Text,labels " Anthu aphunzitsidwe zauindo wawoNice Bungwe la National Initiative for Civic Education (Nice) Public Trust lati dziko lino likulephera kutukuka chifukwa choti anthu ambiri sadaphunzitsidwe za ufulu komanso udindo wawo pa zinthu zosiyanasiyana, kuphatikizapo ntchito za chitukuko. Mkulu wa Nice Trust, Ollen Mwalubunju, ndi yemwe adanena izi Lolemba potsegulira maphunziro a masiku atatu a ogwira ntchito zophunzitsa anthu kubungweli. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Maphunzirowa adachitikira mboma la Blantyre ndi thandizo lochokera ku bungwe la mgwirizano wa maiko a ku Ulaya la European Union (EU). Mwalubunju adatsindika kuti, kwa zaka zingapo, boma lakhala likugwira ntchito zachitukuko popanda kupereka mpata kwa nzika kuti zitengepo gawo pa ntchitozo. Choncho, mpofunika kuti boma komanso mabungwe ngati ife a Nice Trust lichilimike pophunzitsa anthu za maufulu omwe ali nawo komanso ndi udindo womwe ayenera kusenza kuti chitukukocho chitheke, iye adatero. Mwalubunju adapempha ogwira ntchito zophunzitsa anthu mmaboma kuti akhale patsogolo pa ntchitoyi. Ife a Nice Trust tili ndi kuthekera konse pantchitoyi potengera ntchito yomwe takhala tikugwira pophunzitsa anthu zachisankho mmbuyomu, adaonjeza. Mkuluyo adathokoza bungwe la EU kaamba ka thandizo lomwe lidapereka kuti Nice Trust igwirire ntchito zake zophunzitsa anthu kwa zaka zingapo. ",10 " Aoloka yorodani pamtsinje wa ruo Sukulu adalekera sitandade 4, kuwerenga nkomuvuta, koma kuwerengera ndalama kwa iye si nkhani. Ngakhale sukulu sadapite nayo patali, ntchito zake zikuthandiza anthu oposa 15 000 kwa T/A Mlolo mboma la Nsanje. Chisale watuluka nkumangidwanso Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Ndi manja ake, mnyamatayu wamanga mlatho wa mamita 100 pamtsinje wa Ruo womwe anthu ambiri tsopano akuolokerapo tsiku ndi tsiku. Mavuto atha: Ana asukulu, abizinesi ndi opita kuchipatala tsopano akutha kuoloka Ruo Nzoonadi, aja adati wopusa adaimba ngoma, ochenjera navina sadaname, tikatengera nkhani ya Laitoni Anoki, wa zaka 28, yemwe amachokera mmudzi mwa Khasu. Ngati ena poyamba ankamutenga ngati wopanda phindu kaamba koti sukulu adatulukira pawindo, lero wasanduka momboli wawo. Ngakhale mafumu mderali akuvomereza kuti Anoki ndi ngwazi ya anthu kumeneko. Njinga zamoto, zakapalasa komanso matumba a chimanga ndi zigubu za mafuta zikuoloka pamenepa popanda vuto. Zonse zidayamba ndi madzi osefukira amene adavuta chaka chino. Chifukwa chosefukira mtsinje wa Ruo udaiwala khwawa nkuphotchola. Midzi yambiri idakokoloka, anthu makumimakuni adafa pangoziyo, osanena za ziweto ndi kukokoloka kwa minda. Mtsinjewu udachititsa kuti anthu azilephera kupita kuchipatala ku Makhanga Health Centre, kusukulu yasekondale ya Makhanga, komanso kumsika wa Admarc mderali. Mtsinjewo wachitanso malire ndi dziko la Mozambique komwe anthuwa amapitako kukasuma chimanga kutsatira njala yomwe yagwa mbomali komanso ndiko kukuchokera mafuta ophikira. Poyamba, anthuwa ankangoyenda osaoloka mtsinje chifukwa padalibe mtsinje. Ankaoloka Ruo pokhapo ngati akupita ku Mozambique. Anthu a derali, kudzera mwa mafumu awo, akhala akupempha mabungwe komanso boma kudzera mwa phungu wawo Esther Mcheka Chilenje kuti awamangire mlatho pa Ruo koma kuli chuu. Ngoziyi itangochitika, phungu wathu adabwera kudzationa ndipo adatitsimikizira kuti atimangira mlatho poona kuti sitingathenso kupita kuchipatala ndi madera ena. Koma mpaka lero sitikudziwa kuti lonjezoli litheka liti, adatero gulupu Manyowa. Adadza ndi nzeru zomanga mlatho: Anoki Manyowa akuti anthu pafupifupi 15 000 ndiwo akhudzidwa mwa magulupu 13 onse a mwa T/A Mlolo. Ataona kufunika kwa mlatho pamtsinjewu Anoki, ngati wamisala, adayamba kudula mitengo nayamba kukhoma mlathowo. Pocheza ndi Msangulutso, mnyamatayu akuti adayamba ntchito yomanga mlathowu mvula ili pafupi kusiya, apo nkuti madzi akulekeza mkhosi. Poona kuti ntchito indikulira ndidakopa anyamata ena kuti tithandizane. Tidalipo 8. Tidadula mitengo ndipo ina ndimachita kugula. Ndidakagula misomali, ina anthu adangotipatsa koma ina ndidachita kukongola pamtengo wa K40 000. Zida zitakwana, tidayamba kukhoma mitengo pamadzipa. Timasongola kaye mitengoyo ndi kukhoma ndi hamala. Ntchito idalipo chifukwa madzi nkuti ali ambiri moti mwina amandilekeza mkhosi, adatero Anoki. Pakutha pa miyezi itatu, mlatho wotalika ndi mamita 100 nkuti utatha ndipo anthu adayamba kuolokerapo. Ngakhale tidamaliza komabe tsiku lililonse timaugwiragwira chifukwa pena umapeza msomali wazuka kapena mtego wachoka chifukwa pamadutsa anthu ambiri, adatero. Lero Anoki wayamba kudyerera thukuta lake pamlathowu. Munthu mmodzi amalipira K100 kupita ndi kubwera. Njinga yamoto timalipitsa K200, thumba lolemera ndi makilogalamu 50 timalipitsa K100, koma opita kuchipatala sitimawalipiritsa. Patsiku Anoki akuti amapanga ndalama yosachepera K20 000. Sungadabwe kumuona mnyamatayu lero akutuluka mnyumba yanjerwa zootcha komanso yamalata, ndipo wagula mbuzi zingapo, kumunda waikako aganyu. Kupatula apo, Anoki walemba ntchito anyamata asanu kuti azithandizira pamlathowo. Anthu amaoloka ndi usiku womwe. Komanso pakufunika anthu olondera ndiye pali anyamata asanu amene akuthandiza. Ena amathandizira kuolotsa njinga. Patsiku ndikumawalipira K1 500 aliyense, adatero Anoki. Anyamata amene adamanga nawo mlathowu akulandiranso zawo. Chomwe tapanga nkuti tizigawana sabata yolandira ndalamazi. Sabata ino ndilandira ndineyo, ndiye kuti wina alandira sabata yamawa. Mmene tikuteremu ndiye kuti ndalama yokonzetsera mlathowu imakhalanso tasunga. Mukuona anthu akubweretsa mitengo, amenewa tikufuna tiwagule kuti zida zikhale zokwanira, adatero Anoki, uku akusintha ndalama zopatsa kasitomala. Mphindi 20 zomwe tidakhala pamlathowo, onyamula zigubu za mafuta ndi matumba a chimanga kuchokera mdziko la Mozambique, opita kuchipatala komanso ophunzira ndi alimi ndiwo amaoloka mowirikiza. Lero dzina la Anoki silisowanso mmudzimo. Gulupu Manyowa akuti alibe naye mawu mnyamatayu. Mtsinje umenewu ndi waukulu, anthu 9 a mmudzi mwanga adapita akuoloka mtsinjewu. Lero tikutha kumaoloka mwaufulu, zomwe sitidaziganize chifukwa maso anthu adali kuboma. Izi zidatipatsa chimwemwe. Pano tikumapita kumsika, kusekondale, ku Mozambique komanso ku Admarc mopanda vuto. Simungapite ku Bangula kuchokera kuno osadutsa pamlathowu, adatero Manyowa amene akuti masiku ena samalipitsidwa. Mkulu wina amene ankapita kuchipatala ndi bambo ake adati mlathowu wawathandiza kopambana. Mkuluyu, Gift Filipo, wa mmudzi mwa James kwa Gulupu Mchacha, akuti pachipanda mlathowu sakadapita ndi bambo ake kuchipatalako. ",15 " Ulimi wa mthirira nchuma Tikudziweni Ndine Moffat Mtalimanja ndipo ndi mkazi wanga Effie timachokera mmudzi wa Kaunde, ku Namadidi kwa Senior Chief Mlumbe mboma la Zomba. Ndife alimi amene timaweta ziweto zosiyanasiyana kuphatikizaponso kuchita ulimi wa mbeu zosiyanasiyana. Pa ulimi wa mbeuzi timachita onse wa mvula komanso wa mthirira. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Ulimi wa mthirira mudauyamba liti? Ulimiwu tidauyamba mzaka za mma 1970 pamene bambo amagwira ntchito ku Portland Cement ku Changalume. Chimene chidatiyambitsa kuchita ulimiwu ndi kupewa kugula ndiwo za masamba omwe zimene timaona kuti tikhonza kuzikwanitsa kumazilimira ndi kumadzidyetsa tokha. Mkati mwa njira ndi pamene tidaona kuti mbeu za masambazi ndi mpamba waukulu chifukwa anthu ozungulira kuno adayamba kumabwera kumatigula ndi pamene tidaonjezera moto kumachita ulimiwu mwakathithi. Ndi mbewu ziti zimene mumalima? Masambawo amafunika kuthirira Tomato, kabichi, anyezi, beetroot, brocolli, nyemba, chimanga ndi mbeu zina zambiri malinga ndi kukonda kwa anthu ogula. Kuchokera 1970 pali mtunda ndithu, chinsinsi chake chagona pati kuti muzilimabe mpaka pano? Ulimi wa mthirira uli ndi chuma chobisika chimene alimi ambiri sanachitulukire. Mnyengo ya mvula, mbeu zambiri zikalimidwa ndipo zikakhwima pamsika zimakhala mbweee ndipo zimagulitsidwa pa mitengo yolira pamene mnyengo yopanda mvula ndi mmene za masamba zimakhala zochepa koma ogula ndi ambiri. Apa mpamene mlimi wa nzeru amayenera kugwira mpini. Ndi phindu lotani limene mumapeza mu ulimiwu? Phindu limene timapeza mulimvetsetse ndi kuwerengera kuti anthu pakutha pa mwezi amagwiritsa ntchito ndalama zingati pogula tomato ndi masamba kuti azidya tsiku ndi tsiku pakhomo pawo. Mukhoza kuona kuti amagwiritsa ntchito ndalama zambiri zimene akanati masambawa alima okha ndiye kuti ndalama zimenezi akanapangira zinthu zina zofunika pakhomo pawo. Pachifukwa chimenechi, sitigula chilichonse chokhudza masamba komanso timagulitsa masambawa kusonyeza kuti timapha mbalame ziwiri ndi ulimi wa nthilirawu. Pa chifukwa ichi ndalama zimene taziteteza posagula masambazo timapangira chitukuko chosiyanasiyana pakhomo pathu pano. Ndi zovuta zotani zimene mukukumana nazo ndipo mumathana nazo motani? Vuto lalikulu ndi madzi. Malo amene timalimawa tidayetsetsa kusaka madzi kuti tikumbe chitsime koma madzi sanapezeke. Kotero madzi adapezeka patali ndithu pamene tinakumba chitsimecho choncho tinalemba ntchito anthu amene amakatunga madzi pa chitsimepo ndikumazathira mu migolo imene timatungamo ndi kumathilira mbeuzi. Pakadali pano tili ndi malingaliro opeza makina opepera madzi amene adzipopa madzi pachitsimepo ndikumabweretsa ku dimba kuno kuti ulimiwu ufike pa mponda chimera. Ulimi wa mthirira uli ndi phindu? Kwambiri. Mwachitsanzo, talima tomato mitengo 650. Ndipo mbeu yakeyi imabereka bwino chifukwa imatha kubereka tomato osachepera 50. Ndiye pa mitengo 650 mtengo uliwonse ubereke tomato osachepera 50 ndiye mwachitsanzo tomato mmodzi adzigulitsidwa K50 mukapanga masamu mukupeza bwa? Komanso kabichi amene timalima ndi mbeu yaikulu bwino amene mmodzi timagulitsa K250 ndiye ngati tadzala oposa 100 mukhoza kuona kuti paphedwa makwacha ochuluka bwanji? Chimanga chachiwisi nacho cha nthilira chikachita bwino chimasanduka chitsulo cha ndege pa msika, kotero ngati walima chochuluka mlimi satola chikwama? Mbeu zina monga nyemba, tanaposi, beetroot, brocolli nazo ndi golide kale mchilengedwe chake kotero ngati mlimi akulima zimenezi mwakathithi umphawi ungakhale ndi ulamuliro pa moyo wake? Ngati dziko titani kuti ulimi wa nthilira udzipindulira dzikoli? Chofunika alimi asinthe kaganizidwe ndipo avomereze kuti ulimi wa nthilira ndi ulalo opititsa chuma chawo chomwe komanso cha dziko pa tsogolo. Zimatiwawa kumaona munda umene uli pafupi ndi msinje wakuti suphwera koma palibe chikulimidwapo kudikilira mvula basi uku kumakhala kuseweretsa ndalama. Boma komanso mabungwe amene amalimbikitsa ulimi ayedzeke chidwi chawo powapatsa mphamvu alimi ndi zipangizo zimene zingatakasile ulimi wa nthilira kuti upite pa tsogolo chifukwa nthaka ndi madzi mdziko muno ndi zambiri. Ngati ife tikukwanitsa kuchita ulimi ndi madzi a pa chitsime tsono amene minda yawo ili pafupi ndi madziyo angapindule bwa? Tilimbikitsenso achinyamata kuti pamene akusakasaka ntchito zamu ofesi aganizirenso zochita ulimi chifukwa ulimi ukhoza kusintha miyoyo yawo nkuthwanima kwa diso. Ndi ubwino wotani umene ulipo ochita ulimi ngati banja? Pamakhala kudalirana kwakulu, mwachitsanzo, ulimi umenewu amene amakhala patsogolo ndi mayi ndipo ine ndimangothandizira mapeto ake nzeru zawo ndi zanga tikaziphatikiza pamodzi ndi zimene zimachititsa kuti zinthu zizitiyendera bwino chotere. Muli mphamvu mukudalirana. ",2 " Wa gulewamkulu atuluka pa belo Bwalo la milandu mboma la Kasungu lapereka belo kwa munthu yemwe adayerekeza kuvala gulewamkulu ndipo akuganiziridwa kuti adagwirira mwana wa zaka 7 pomwe mwanayu amachokera kusukulu pamodzi ndi anzake ena awiri pa mtsinje wa Mkazimasika mbomalo. Gule wa mkulu Apolisi a mbomalo adagwira mnyamata wa zaka 16 ndi kumutsekera mchitokosi sabata ziwiri zapitazo pomuganizira kuti ndiye adapalamula mlanduwo atavala gulewamkulu. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndipo mnyamatayu adadziwika chigoba chomwe adavala chitagwa pomwe adali mkati mogwirira mwanayo. Malinga ndi mneneri wa polisi mbomalo Harry Namwaza, mnyamatayu adavomera kuti adapalamula mlanduwo pamaso pa woweruza milandu Damiano Banda. Namwaza adati pakadalipano mnyamatayo wapatsidwa belo poyembekeza lipoti kuchokera ku nthambi ya boma yowona za chisamaliro cha anthu. Malinga ndi malamulo oteteza ana mdziko muno, mwana saweruzidwa pamlandu nthambi ya bomayo isanapereke lipoti lokhudza mwana amene wapalamula mlandu. Koma mkulu wa nthambiyo mboma la Kasungu, John Washali adati sakudziwa kalikonse za nkhaniyo ndipo sadalembe lipotilo. ",7 "Apolisi, Asilikali Ati Akhwimitsa Chitetezo mu Nthawi Yosayendayenda Apolisi mdziko muno mogwirizana ndi asilikali a nkhondo, anenetsa kuti apereka chitetezo cholimba motsatira malamulo a dziko lino amene amawalora kuti awonetsetse kuti mdziko muli bata ndi mtendere komanso kuti aliyense akutsatira malamulo. Anayitanitsa msonkhano wa atolankhaniwo-Mwapasa Wogwilizira udindo wa mkulu wa apolisi mdziko muno a Danken Mwapasa limodzi ndi mkulu wa asilikali a nkhondo mdziko muno a Peter Lapken Mathanga anachititsa msonkhano wa atolankhani omwe wachitika lachinayi mu mzinda wa Lilongwe, pokonzekera masiku 21 osayendayenda omwe pulezidenti Peter Mutharika walengeza kuti ayambira pakati pa usiku wa loweruka sabata ino mpaka pakati pa usiku wa pa 9 May chaka chino. Nthambi ziwirizi zapempha anthu mdziko muno kuti atsatire bwinobwino malamulo omwe aikidwa ponena kuti opezeka akuyenda mopanda chilolezo adzalangidwa moyenera monga waphwanyira malamulowa. Pamenepa atolankhani anafunitsitsa kudziwa kuti anthu adzalandira chilango chotani potengera kuti ndendenso za dziko lino, potengera nkhani ya Corona Virus yomweyi sikukuyenera kuti kudzaze. Iwo anayankhapo kuti anthuwa adzatengeredwa kupolisi ndipo mwachangu adzakawonekera ku bwalo la milandu komwe adzikalandira chilango mwachangu. Nkhani ina yomwe inamanga nthenje kumeneku ndiyokhudza ntchito zakumunda pamene anthu ena akukololabe mbeu zawo. Pamenepa akuluakuluwa ati mpofunika anthu afunse komwe akuyenera kuti akatenge chilolezo choti agwirire ntchitozo momasuka. Iwo anenetsanso kuti sikufuna kwawo kuti adzagwire ntchito yawo mwa nkhanza koma mokhala kumbali ya wanthu komanso anenetsa kuti anthu akuyenera kutsatira malamulowa kaamba koti ndi anthu omwewo amene apindule ndi mfundozi. ",7 "World Vision Yapempha Anthu Alimbikitse Ukhondo Bungwe la world vision mboma la Dedza lati anthu akuyenera kumadzisamalira nthawi zonse pofuna kupewa kachilombo ka Coronavirus. Mkulu wa bungweli mboma la Dedza a Thokozani Chibwana amalankhula izi pomwe bungweli limapereka katundu wosiyanasiyana pa chipatala cha Dedza wa ndalama zosachepera 13 Milion Malawi Kwacha. A Chibwana ati bungwe la World Vision ndilokhudzidwa ndi mmene matendawa akufalikira ndipo anawona kuti ndi koyenera kuti achitepo kanthu pofuna kupewa mliriwu. Mukudziwa kuti ntchito imeneyi kuti iyende imafunika kuti tikhale ndi zipangizo zokwanira monga ma Anti-Biotics, ma glove, ndowa ndi zina zambiri zoti zitithandize pa nkhani za ukhondo makamaka madera omwe tikugwiramo ntchito mboma lino, anatero a Chibwana. Mwazina bungweli lapereka mankhwala, ma pail 20, sopo 50, ma glove okwana 7 thousand komanso zovala zozitetezera zokwana 1500 kwa anthu owona za umoyo mbomali. ",6 " Aletsa zionetsero za madzi Mkulu wa bungwe loona za ufulu wa ogula la CAMA John Kapito Lachinayi adalepheretsa zionetsero ngakhale mpaka lero anthu ozungulira Blantyre akusaukirabe madzi. Chionetserochi chidakonzedwa ndi mkulu wa pamene amati ayende kukadandaulira kampani yogulitsa madzi ya Blantyre Water Board (BWB). Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Zionetserozi zimadza pamene kwatha mpaka miyezi iwiri madzi mmadera ena amumzindawu asakutuluka mumzindawu. Koma Kapito adati: Tidakumana ndi akuluakulu a bungweli ndipo atitsimikizira kuti ayamba kupereka madzi. Taona kuti palibenso chifukwa chochitira zionetsero pamene atilonjeza kuti ayamba kupereka madzi, Kapito adauza atolankhani. Koma pofika Lachinayi, madera ambiri mumzinda wa Blantyre madzi adali akuvutabe zomwe zidachititsa anthu ena kukwiya nazo. Mmodzi mwa anthuwo, Rawjazz Siula akuti ndi bwino tsiku lina kudzachita zionetsero zosagwirizana ndi bungwe la Cama popusitsa Amalawi. Basi bwana Kapito akatinamize pamene tikunena kuti patha sabata zambiri madzi asakutuluka? Bwanji sadayitane anthu omwe amawauza kuti ayende pamsewu kuti zionetsero zalephereka? sakumvetsa Siula. Mwayi Mbwelera akuti nkhani ya madzi yavuta kotero zionetsero si bwenzi zitalephereka. Kuno ku Mbayani anthu tikusaukira madzi, nthawi yonseyi bwanji samatibweretsera madziwo? Zalakwika, adatero. ",2 " Zungulizunguli mu Lilongwe Abale anzanga, inetu ukwati, nkhani ya ukwati, sindikamba nawo. Nkhani imeneyi, kwa ine ndimangoionera apo!!! Chifukwa chake nachi: Pali ana ena amene amaganiza kuti mayi awo ndi amami, chonsecho mayi awo ndi anti. Komanso pali ana ena amene amaganiza kuti bambo awo ndi adadi chonsecho ndi ankolo. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Musayerekeze kundifunsa kuti ndikutanthauza chiyani chifukwa sindikuyankhani. Ndakwiya nanu chifukwatu ndili muno mu Lilongwe momwe ndimakumana ndi anyamata ena. Musayerekezenso kundifunsa ngati nkhani yake inali ya ukwati kapena ayi. Mukadziwa mukufuna mutani? Ndidatsika basi ya Lilongwe tsikulo chifukwa Abiti Patuma adandiuza kuti mzindawo uvuta. Abale anzanga nanga nkadatani? Nkadachitanji chifukwatu ena adandiuza kuti uku nkwa gule ndipo ukwatiwo ndi wa abale. Mwinatu sindidakuuzeni. Nthawi ija ankamanga ukwati anyamata aja, nthawi ya Moya Pete, ine ndidali pomwepo limodzi ndi Abiti Patuma. Inde, anyamata aja adatchuka. Chongoti mu Lilongwe fikeni, abale anzanga, inetu zikwama ndimachita kupanira ngati chiyani kaya! Tidayenda kamtunda ndithu ndipo tidaona umo apolisi amatapira ndalama muno mu Lilongwe: Kwa Biwi, inde Lower Biwi! Kugonetsa abambo olemekezeka pansi ati vakabo yawatapula! Umo mu Devils Street, ati kumene chiwanda cha Satana chidafikira, asungwana kukopa abambo; anyamata kufwamba abambo ndipo ana kutoleza zimene ataya abambo. Lilongwe iyooo! Za kwinako sindikamba. Ati Kumpanda kwa Mafumu, inde ku Side kofikira Madonna; apa paakazembe ngakhalenso kumabedi ndiye eeeeh! Nkhani ili apa ndi ya anyamata amene tidawapeza akuchita zawo. Musadandaule, aka si koyamba, komanso kumbukirani anyamata a mu Mchesimu tsiku lina adafuna kuphwanya hotela ati chifukwa mwini hotela adazembetsa ana ena! Lilongwe iyooo! Tsono nkhani yakula apa ndi yakuti Moya Pete tsono wakumana ndi zija adakumana nazo Mfumu Mose nthawi ija ankafunsidwa ngati Mustafa angasiyire mngono wake Ajibu mpando woyanganira ife ojiya, osolola ndi osenza pano pa Wenela. ",15 " Phindu kawawa ndi ulimi wa tsabola Akulipirira ana awiri ku sekondale; wagula mbuzi 19 ndi nkhuku 30. Njinga, ziwiya za pakhomo komanso banja lake silikugona ndi njala. Nkhani ya Jimmy Maliwu, mlimi wa tsabola ku Mulanje ndi chitsanzo kuti ulimi wa tsabolawu ndi kawawa. BOBBY KABANGO akucheza ndi mlimiyu: Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Maliwu: Ndidagulitsa mosavuta Wawa achikumbe Wawa, imani komweko musafike pafupi, kuno ndi kwa alimi okhaokha. Kuli chiyani mukuchita kukanizira? Tikusankha tsabola ndiye mphepo yake inuyo simungayandikire, mukuona aliyense akungoyetsemula. Ndiye tidziwanetu Ndine mlimi wa tsabola, dzina ndine Jimmy Maliwu wa mmudzi mwa Sazola kwa Senior Chief Mabuka mboma la Mulanje. Mudayamba liti ulimiwu? Mu 1999 ndi pamene ndidayamba kulima tsabola. Chidachitika nchiyani kuti muyambe ulimiwu? Pa nthawiyo nkuti ndikulima chimanga komanso mbewu zina. Ndiye ndinkafuna ndichite ulimi wina womwe ndizipezerapo ndalama. Apa ndi pamene ndidasankha tsabola. Chifukwa chiyani mudasankha ulimi wa tsabola? Ndinkafuna ulimi wa fodya, koma kuno sachita bwino. Ulimi wa tsabola ndi omwe ndidaona kuti akuphamo ndalama. Mudayamba bwanji? Ndidalima mizere yochepa, ndimafuna kuti ndione ngati ndingathe komanso ngati msika wake uchite bwino. Zidayenda koma osati kwambiri, ndidaikamo chidwi. Chidayenda nchiyani? Kumunda zidatheka komanso pamsika ndidagulitsa mosavutika ngakhale mtengo wake udali wolira. Mtengo udali bwanji? Ndidagulitsa K39 pa kilogalamu pamene alimi ena amagulitsa K50. Kuchoka 1999 kufika lero, ulimiwu ukuyenda bwanji? Mitengo ndiyo yakhala yovuta koma kumunda ndiye zonse zili bwino. Ndidaonjezera munda ndipo pano ndikulima wokula ndi mamita 35 mulitali ndi 17 mlifupi. Munda umenewu mukukolola wochuluka bwanji? Ndikumapeza tsabola makilogalamu 150 ngati mvula yagwa bwino komanso ngati matenda sadafike. Chaka chatha zidayenda bwanji? Nanga pamsika padali bwanji? Chaka chatha ndidakumana ndi vuto la matenda ndiye ulimi udavuta moti ndidapeza makilogalamu 45 okha chifukwa alangizi adafika mochedwa. Pamsika ndiye zidali bwino chifukwa amagula K2 500 pa kilogalamu. Ndi matenda ati amene adavuta? Tsabola amapanga zilonda komanso mitengo imauma. Zikatere zimakhala zovuta kuti abereke bwino. Panopa matendawa tawakonzekera chifukwa tidali ndi maphunziro a momwe tingathanirane ndi matendawa. Koma vuto lomwe lidalipo kuti tikumane ndi matendawo nchifukwa cha manyowa amene tidagwiritsira ntchito. Tsabola wakupindulirani bwanji? Muli ndalama, chaka chatha ndidapeza K112 500 kuchokera mmakilogalamu 45 amene ndidakolola. Ndagula mbuzi 19 komanso nkhuku 30. Ndili ndi ana atatu, mmodzi ali Fomu 2 wina 4 ndi wina ali ku pulaimale. Onsewa ndalama zake zikuchokera mu tsabola. Sindinagonepo ndi njala chifukwa ulimiwu umandisuntha. Tifotokozereni za kumunda, kuli bwanji pano? Panopa tikuwokera pamene mitengo ya chaka chatha tikuthyolera kuti ipange nthambi. ",4 " Nkhanza za mbanja zikupitirira kuchuluka Mzimayi uyu adakhapidwa ndi mwamuna wake ku Thyolo Ngakhale chaka ndi chaka dziko lino limakhala ndi masiku 16 othana ndi nkhanza mogwirizana ndi maiko ena padziko lapansi, zenizeni sizikuoneka pamene nkhani za nkhanza mmaboma zakula msinkhu. Malinga ndi mneneri wa polisi Rhoda Manjolo, mu 2013 anthu 4 499 adachitiridwa nkhanza kuchokera mwezi wa January mpaka June. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Chaka chino, Manjolo wati kuyambira January mpaka September nkhani zotere zakwana 9 842, chomwe ndi chiwerengero chokwera kuyerekeza ndi 2013. Nkhani zoti mayi waphedwa ndi mwamuna wake kapena bambo waphedwa ndi mkazi wake nazonso zakhala zikumveka. Komatu izi zikuchitika pamene chaka ndi chaka amabungwe padziko lapansi amakhala ndi kampeni yomemeza anthu kuti asiye nkhanza kuyambira pa 25 November mpaka pa 10 December. Lipoti lomwe unduna wa za jenda ukuyembekezereka kutulutsa sabata ikudzayi ukusonyeza kuti nkhani zophana ndizo zidakula msinkhu mchakachi. Mlembi muundunawu, Dr. Mary Shawa, dzana Lachinayi adakana kuuzaTamvanizomwe zili mlipotimo ponena kuti tidikire sabata ikudzayi. Sindinganene momwe nkhanza zachitikira mchaka chino, komabe pali kusintha kuti anthu akutha kukanena kupolisi akachitiridwa nkhanza. Abambo tsopano ayamba kukadziwitsa apolisi pamene achitiridwa nkhanza, adatero Shawa pokambapo pangono za lipotilo. Chaka chino ndiye pali nkhani zophana zoposa zisanu. Iyi ndi nkhani yachisoni kwambiri komanso tidali ndi nkhani yomwe amayi atatu adagwiririra mnyamata wa zaka 13; abambonso aphedwa ndi akazi awo. Mumva zambiri tikatulutsa lipotili pa 9 December pano, adawonjeza Shawa. Mkulu wa bungwe lomwe limalimbana ndi kuthetsa nkhanza la Umunthu Foundation, David Odali, adati nzachisoni kuti nkhanza zikungochulukira ngakhale iwo ali kalikiriki kudziwitsa anthu kuti asiye mchitidwewu. Nzachisoni kumamva nkhani ngati izi pamene ife tikuyenda maboma onse kudziwitsa anthu koma nkhanza zikupitirirabe, adadandaula Odali. Koma Odali akuti pali mfundo zinayi zomwe zikuchititsa kuti mchitidwewu ukhale ukukulirabe. Iye wati mchitidwe wa amayi ena amene amati akavulazidwa ndi amuna awo amakathetsa nkhani kubwalo kuti isapitirire ndicho chimodzi chikuchititsa kuti mchitidwewu uzipitirira. Munthu amuvulaza koma akuti nkhani ithe ponena kuti ndi mwamuna wake, kodi izi zingapereke phunziro lanji? Amayi aphunzire kulolera kuti lamulo lizigwira ntchito yake ngati munthu wawavulaza, adatero Odali. Iye adati mfundo ina ndi kuti anthu ena salolanso kuti nkhani zotere zikachitika zizikanenedweza kupolisi ponena kuti ndi nkhani ya mbanja yomwe imayenera ikambidwe ndi bambo kapena mayi wa pabanjapo. Odali watinso ndi bwino abambo azikanena kupolisi ngati achitiridwa nkhanza. Abambo ena akachitiridwa chipongwe ndi mkazi wawo samanena, iwo amati akupirira koma akuchulukitsa mchidwewu. Pasakhale kupirira pakati pa abambo, adatero. Komabe iye adayamika kuti ngakhale nkhanzazi zikutenga malo, anthu ambiri aphunzira kumakanena kupolisi pamene achitiridwa nkhanza kusiyana ndi kale pamene zimathera mnyumba kapena kwa amfumu a deralo. Ndipo polankhula pomwe bungwe la amayi a Chikhristu la Young Women Christian Association (YWCA) limakhazikitsa ntchito yothandiza asungwana kuzindikira za ubereki ku Mulanje Loweruka, nduna ya za jenda, Patricia Kaliati, adati nkhanza kwa amayi ndi asungwana zikuchuluka kwambiri. Iye adati amayi ambiri akuchitiridwa nkhanza chifukwa chosowa maphunziro. Asungwana ambiri atalimbikira maphunziro, nkhanza zikhoza kuchepa chifukwa akhoza kuzindikira ufulu wawo. Nchifukwa chake tikubweretsa lamulo lakuti ana asamakwatiwe asanafike zaka 18. Mafumu ali ndi udindo waukulu woteteza ana pokhazikitsa malamulo apadera. Mwachitsanzo, madera ena mafumu adakhazikitsa malamulo akuti makolo amene akusiyitsa ana sukulu kuti akakwatiwe amalipitsidwa dipo, adatero Kaliati. ",15 "Maepiskopi Akatolika Awunikira Akhritsu Awo za Mtsogoleri Woyenera Kumusankha Maepiskopi a mpingo wa katolika mdziko muno atulutsa kalata yomwe mwa zina yaunikira dziko ndi akhristu a mpingowu zina mwa zomwe akuyenera kudziunika pofuna kukonza maziko abwino a dziko ndi miyoyo yawo. Kalatayi yayamba ndi mau a mbukhu loyera kuchokera pa Mateyo mutu wa 20 kuyambira ndime ya 25 mpaka ya 27, pomwe pali mawu akuti Yesu adawaitana ophunzira ake nawauza kuti mukudziwa kuti olamulira amadyera anthu awo masuku pa mutu. Koma pakati pa inu zisamatero ayi. Aliyense ofuna kukhala wamkulu akhale mtumiki wanu ndipo aliyense wofuna kukhala mtsogoleri pakati panu, akhale kapolo wanu. Alemba chikalatacho-Maepiskopi aku Malawi Malinga ndi kalatayi yomwe mutu wake ndi kusindika za kufunika kosintha zinthu ndi kuyambanso moyo watsopano mMalawi, yalimbikitsa anthu kuti atenge gawo posintha zinthu mdziko muno. Chisankho chatsopano cha mtsogoleri wa dziko chomwe chikudzachi ndi njira imodzi yomwe aMalawi angasinthire zinthu zomwe zakhala zisakuyenda bwino. Ofunika kusankha atsogoleri okhawo omwe angathandize aMalawi kuti akhale amodzi ndi ogwirizana, ochita zinthu mwadongosolo, owopa Mulungu, olemekza malamulo a bwalo la milandu komanso osakondera chigawo kapena chipani, chatero chikalatacho. Iwo adandaulanso ndi khalidwe losankhana mitundu lomwe lakhala likuchitika, zipolowe pa ndale komanso kuchuluka kwa katangale ndi kusalangidwa kwa anthu akaphwanya malamulo ndipo alimbikitsa kampeni yamphamvu yothana ndi nthenda ya COVID-19. Kalatayi ndi ya namabala 26 kulembedwa ndi maepiskopi a mpingo wa katolika mdziko muno kuchokera mu 1961 pomwe analemba kalata yoyambilira. ",11 " Agundidwa akuthawitsa katundu wakuba Bambo wina wagundidwa ndi galimoto ku Mzuzu pomwe amathawitsa mapaketi awiri a khofi omwe amamuganizira kuti adaba pa Mzuzu Coffee Den. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Bamboyo, yemwe ndi Laston Kaunda wa zaka 32 ndi wochokera mmudzi mwa Chiphanzi, T/A Nkumbira mboma la Nkhata Bay. Mneneri wapolisi mumzinda wa Mzuzu, Patrick Saulosi, adati mnyamatayo adapita ku Coffee Den mmawa wa Lachiwiri sabata yatha ndi nsuweni wake komwe adakanyamula mapaketi a khofiwo. Woganiziridwayo akutuluka mu Coffee Den muja adatuluka ndi mapaketi awiri a khofi osalipira. Mnyamata wogwira ntchito pamalopo ataona zomwe amachita Kaunda adayamba kumuthangitsa, adafotokoza Saulosi. Saulosi adati pa nthawi yomwe Kaunda amafuna kuoloka nsewu galimoto idamuomba ndipo iye adavulala kwambiri mwendo. Iyeyo ali kuchipatala cha Mzuzu Central Hospital (MCH) koma akangotuluka kuchipatalako atengedwa ndi apolisi pamlandu wakuba, adatero Saulosi. Saulosi adati kaamba ka kuchepa kwa mlanduwo palibe wapolisi amene akudikirira Kaunda kuchipatala podikirira mlandu. Msangulutso utapita kuchipatalako udakumana ndi Kaunda yemwe akadali mchipatala kulandira thandizo. Kaunda adati sakukumbukira chilichonse chomwe chidachitika patsikulo chifukwa adali ataledzera kwambiri. Sindikudziwa chomwe chidachitika ndidangozindira kuti ndili kuchipatala kuno, iye adayankha motero. ",7 " Apolisi sakununkha kanthu pa chitetezo Ngombe zayangana kudazibomu! Ubale wa anthu ndi apolisi wafika pa wa mphaka ndi galu moti apolisi sakununkhanso kanthu pa ntchito yawo yoteteza anthu ndi katundu wawo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Asirikali a Malawi Defense Force kusungitsa mtendere pa zionetsero Sabata zitatu zapitazo agogo 6 adaphedwa mboma la Karonga powaganizira kuti ndi athakati. Apolisi atapita kuti akagwire anthu omwe adachita izi, adawathamangitsa ndi miyala, mipini, mipaliro ndi zibonga moti adalephera kukwaniritsa zolinga zawo. Aka sikadali koyamba izi zichitike mbomalo. Chaka chathachi apolisi kwa Nyungwe adamenyedwa ndi anthu atatsekera anthu omwe adakatenga namulondola kuti adzawathandize kugwira mfiti mderalo. Nako ku Ntchisi anthu okwiya adapha agogo awiri powaganizira kuti adalodza mnyamata wina wa zaka 15 mmatsenga. Ngakhale izi zidachitika mwezi wa October chaka chatha, mneneri wa polisi mbomalo Richard Kaponda wauza Msangulutso kuti mpaka lero palibe yemwe wamangira mokhudzana ndi nkhaniyo. Nako ku Neno komwe anthu adapha nkhalamba zomwe amaziganizira kuti ndi mfiti, apolisi adachita chidodo kuti akagwire ndi kuzenga mlandu anthu omwe adachita izi. Anthu adali ndi mkwiyo waukulu moti apolisi amachita mantha kuti awagwire. Nazo zionetsero zosonyeza kukwiya ndi momwe bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) lidayendetsera chisankho cha mtsogoleri wa dziko lino zaikanso pambalambala kufooka kwa apolisi moti boma lidapempha asirikali a nkhondo a Malawi Defense Force (MDF kuti awathandize kuteteza anthu ndi katundu wawo. Mkulu wa apolisi Duncan Mwapasa adavomera pa msonkhano wa atolankhani kuti apolisi ali ndi mphamvu zochepa ndipo sangakwanitse kuteteza anthu omwe akuchita zioneserozo. Apolisi akhala akuona mbwadza pa zionetserozo. Mmalo moti apolisi azisaka amtopola, anthuwo ndiwo akumasaka apolisi nkumawavula, kuwamenya, kuwalanda mfuti, kuwatsatira mmakomo nkukachita chipongwe mabanja awo moti wapolisi wina, Imedi Usumani, adaphedwa. Kuphwando la kumapeto a chaka chino, mkulu wa apolisi wa mchigawo chakummwera Sladge Yousuf adati ntchito yoteteza anthu ikuvuta kaamba kakusakhulupirirana pakati pawo ndi anthu akumudzi. Yousuf adati chodandaulitsa kwambiri ndi kuphwanyidwa, komanso kuotchedwa kwa mapolisi mdziko muno. Amalawi okwiya akumatsatira munthu yemwe ali mchitokosi mpaka kukaphwanya kapena kuotcha polisi nkumutulutsamo. Nkhamenya ku Kasungu ndi Chilobwe ku Blantyre ndi ena mwa mapolisi omwe adaphwanyidwa kaamba kosemphana Chichewa pakati pa apolisi ndi anthu akumudzi. Mmodzi mwa aphunzitsi a pa sukulu ya ukachenjede ya University of Livingstonia George Phiri adati apolisi asuluka chifukwa cha katangale, komanso utsogoleri wa dziko lino omwe wakoledzera moto kuti ntchito. Phiri adati kwakhala kukutuluka malipoti ambiri a katangale yemwe apolisi amachita zomwe zamachititsa kuti Amalawi asowe chikhulupiriro mwa apolisi. Tsopano nkhani za katangale zonsezi zikatuluka, tikuona kuti palibe chomwe atsogoleri akuchitapo pofuna kuthana naye. Pachifukwa ichi anthu angoganiza zotengera malamulo mmanja mwawo, iye adatero. Phiri adati pakadali pano nzovuta munthu kuthawira ku polisi kuti ukapezeko chitetezo chifukwa anthu akakwiya, akumathamangitsa omangidwayo komanso apolisi omwe akumuteteza. Atsogoleri a dziko lino akufunika kuti apeze njira zobwenzeretsa chikhulupiriro cha anthu mwa apolisi, iye adatero. Mwapasa atakumana ndi aphungu a chizimayi a ku Nyumba ya Malamulo pa nkhani yoti apolisi ena adagwiririra amayi ku Mpingu, Msundwe ndi Mbwatalika ku Lilongwe, adavomera kuti pali kusakhulupirirana pakati pa apolisi ndi anthu ndipo ayetsetsa kubwezeretsa chikhulupiriro mwa anthu pogwira ntchito mwachilungamo. ",7 "Papa Wapempha Mabungwe Achilimike Polimbana Ndi Mchitidwe Wogwiritsa Ntchito Ana Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wapempha maiko ndi mabungwe kuti achilimike pa ntchito yolimbana ndi mchitidwe wogwiritsa ntchito ana. Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican, Papa walankhula izi lachitatu ku likulu la mpingowu ku Vatican. Iye wati ndi udindo wa aliyense kuchitapo kanthu pofuna kuthetsa mchitidwe woipa wogwiritsa ntchito ana womwe ukukulirakulirabe chifukwa cha umphawi. Mzolankhulalankhula zake lachitatu Papa Francisco wati ndi wokhudzidwa ndi mchitidwe wonyasa wogwiritsa ntchito ana ntchito zomwe sizigwirizana ndi msinkhu wawo kotero kuti ana amasanduka akuluakulutu nthawi yao isanakwane. Pamenepa iye wapempha maiko ndi mabungwe kuti achilimike polimbana ndi mchitidwewu ndipo waonjezeranso kunena kuti ndi ntchito ya munthu aliyense kuyetsetsa kuchitapo kanthu polimbana ndi mchitidwewu. Papa Francisco wati nthenda monga ya COVID-19 yomwe yakhudza dziko lonse la pansi yabweretsa mavuto osiyana-siyana ndipo yakakamiza ana ambiri mmaiko osiyana-siyana kuti anke nagwira ntchito zoposa msinkhu wao pofuna kuthandiza mabanja awo omwe ali mu umphawi wadzaoneni. Iye wati ntchito zolemetsa zomwe ana akugwira ndi zochititsa kuti matupi awo aonongeke komanso makamaka nzoononga ndi kusokoneza maganizo awo. Papayu wati ana ndi chiyembekezo cha mabanja komanso maiko awo kotero kuti akuyenera kuyanganiridwa bwino. Uthenga wa Papa Francisco wabwera pa nthawi yoyenera pomwe lachisanu pa 12 June, 2020 dziko lonse la pansi likhale likuganizira za mchitidwe wogwiritsa ntchito ana World Day Against Child Labour. ",14 "Phungu Wakale Akagwira Ukayidi Chifukwa Cha Katangale Bwalo la milandu ku Zomba lalamula phungu wakale wa nyumba ya malamulo mdera la Zomba Malosa Anderson Undani kuti akakhale ku ndende kwa chaka chimodzi ndi theka pa mlandu wa katangale. Wasayinira kalatayo-Ndala Malinga ndi kalata yomwe bungwe lothana ndi katangale ndi ziphuphu mdziko muno la Anti-Corruption Bureau (ACB) latulutsa, yomwe yasayinidwa ndi wofalitsa nkhani wake Egritta Ndala, phungu wakaleyu komanso omuthandizira wake Pangani Nazombe anasokoneza ndalama za thumba la Contsituency development Fund (CDF) zomwe zimayenera kugwiritsidwa ntchito pomanga nyumba ya mphunzitsi pa sukulu pulaimale ya Mapalo. Ndalama zina akuti zinali zoti amangire zimbudzi pa sukulu ya Domasi CCAP, kukonzanso nsewu wa Domasi-Kasonga komanso kumanga mlatho pa mtsinje wa Malonga. Bungwe la ACB linamanga awiriwa pa 1 October mchaka cha 2018. Awiriwa anatengeredwa ku bwalo la milandu komwe a Undani amayankha mlandu wogwiritsa ntchito ofesi yawo molakwika, kuba komanso kupeza ndalama kudzera mu njira yachinyengo. Pomwe a Nazombe amayankha mlandu wothandizira munthu kupalamula mlandu komanso kupeza ndalama kudzera mu njira yachinyengo. Pa 3 July bwaloli linawapeza olakwa pa nkhaniyi ndipo pa 13 ndi pomwe bwaloli lapereka chigamulo chake pa nkhaniyi pomwe a Undani alamulidwa kukakhala ku ndende kwa miyezi 18 pa mlandu uliwonse omwe anapalamula. Pamene a Nazombe alamulidwa kukakhala ku ndende kwa miyezi 12 pa mlandu uliwonse omwe anapalamula ndipo akuti chilango chonsechi chidziyendera limodzi. ",7 " Akufuna mayankho pa njala ya mzipatala Mabungwe omwe si aboma ku Rumphi ati akudikirabe yankho kuchokera kwa mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika pa zakusowa kwa chakudya mzipatala zosiyanasiyana mdziko muno. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mwezi wathawu, mabungwe omwe ali pansi pa Civil Society Network ku Rumphi adachita zionetsero ngati njira imodzi youza boma kuti lichitepo kanthu pa zakusowa kwa chakudya pachipatala cha Rumphi. Banda kuwerenga chikalata chomwe adalembera boma Mabungwewa adauza Mutharika, kudzera mchikalata chomwe adapereka kwa akuluakulu a boma, kuti awayankhe pasanadutse sabata ziwiri. Wotsogolera mabungwewa, Eunice Banda, wauza Tamvani kuti boma silinayankhebe chikalata chawocho. Iye wati mabungwewa akufuna kukhalanso pansi kuti apeze njira ina yopezera mayankho kuchokera ku boma. Titachita zionetsero boma lidapereka matumba 100 a chimanga. Koma chakudya chimenechi chitha kumapeto a mwezi uno. Izi zikutanthauza kuti kukhalanso njala kuyambira mwezi wamawa, adatero Banda. Nduna ya za masewero ndi chikhalidwe, Grace Chiumia, masiku apitawa adauza mabungwe kuti achepetse zionetsero chifukwa chakuti boma limamva kamodzi. Chiumia, polankhula ku Nkhata Bay pamene amakhazikitsa ntchito zolimbana ndi nkhanza mbanja, adati ndalama zomwe mabungwe akugwiritsa ntchito pazionetsero azipititse kuntchito zachitukuko. ",6 "Bishop Tambala Apempha Akhristu Asamalire Atumiki Wolemba: Thokozani Chapola ontent/uploads/2019/11/bishop-tambala.jpg"" alt="""" width=""310"" height=""362"" />Tambala: Asisteri amasowa kusamalidwa komanso chitetezo Episkopi wa dayosizi ya Zomba ambuye George Desmond Tambala loweruka wapempha akhristu kuti aziwonetsa chikondi posamalira atumiki mu mpingowu. Iwo amalankhula izi ku Domasi parish pa mwambo wa misa yotsegulira nyumba ya sisteri a chipani cha Our Lady Of Mercy chomwe achikhazikitsa kumene mu dayosiziyo. Iwo ati asisteriwa afika ku parishiyi kuti adzatumikire choncho akhristu nawo akuyenera kuwasamalira mu njira zosiyanasiyana. Tisangowona kuti asisteri abwera kuzatitumikira koma monga anachitira Abraham, asisteri amasowa kusamalidwa monga chitetezo chawo komanso kuwathandiza kuti ntchito yawo agwire bwinobwino, anatero Ambuye Tambala. Ambuye Tambala ati ndi okondwa ndi kufika kwa asisteriwa mu dayosiziyi kaamba koti athandiza kupeputsa ntchito yaikulu yomwe ili mu dayosiziyi. Ndine okondwa kwambiri chifukwa linali khumbo lathu komanso akhristu kwa nthawi yaitali kuti tikhale ndi asisteri chifukwa ntchito ya mmunda mwa Ambuye yakula ansembe sakanatha pawokha kufikira anthu onse komanso utumiki womwe abweretsa kuno ndikuwona kuti ndi wofunika kwambiri, anatero Ambuye Tambala. Chipanichi chili ndi likulu lake mdziko la Italy koma chikupezeka mmayiko osiyanasiyana. ",13 "Zigawenga Zapha Alonda Awiri pa Estate ku Mangochi Apolisi mboma la Mangochi akusakasaka anthu omwe sakudziwika omwe apha alonda awiri komanso kuba katundu wa ndalama zokwana 3.5 million-kwacha pa estate ya Lilimbe mbomalo. Watsimikiza za nkhaniyo Daudi Wachiwiri kwa wofalitsa nkhani za apolisi mbomalo Sub-Inspector Amina Tepani Daudi watsimikiza za nkhaniyi ndipo wati alondawa ndi a Jafali Matola a zaka 72 komanso a Idrissah Ngochela a zaka 66 zakubadwa. Apolisiwa ati anadziwitsidwa izi ndi mlonda yemwe amasintha anzakewa pa ntchito mmamawa pomwe anawapeza akutaya magazi kaamba kovulazidwa ndi akubawa. Ndizoona kuti ife apolisi kuno ku Mangochi tikuyangana anthu omwe aba katundu okwanira 3.5 million komanso apha alonda awiri pa estate ya Lilimbe, anatero Daudi. Iwo atinso apolisi ambomalo adakasakasakabe anthuwo mbomalo ndi cholinga choti akayankhe milandu yomwe apalamulayi. ",14 " Kafukufuku wa chamba watha Zotsatira za kafukufuku wa ulimi wa chamba zomwe Amalawi akhala akudikira zatuluka koma mlembi wa unduna wa zamalimidwe, mthilira ndi chitukuko cha madzi Gray Nyandule Phiri wati zotsatirazi akuzisunga mwachisinsi. Phiri wati zotsatirazi zomwe kafukufuku wake watha zaka zitatu ziyamba zapita ku ofesi ya presidenti ndi nduna zake (OPC) kuti akaziunike zisadaulutsidwe kwa Amalawi. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Kafukufukuyu adatenga zaka zitatu ku Chitedze ndi ku Salima ndipo zotsatira zake zatuluka tsopano koma tikudikira kuti akaziunike ku OPC kenako tidzazitengere ku Nyumba ya Malamulo, adatero Nyandule Phiri. Phungu wa dera la kumpoto kwa Ntchisi Boniface Kadzamira ndiye adabweretsa nkhani yololeza kulima chamba mNyumba ya Malamulo zaka zitatu zapitazo ndipo aphungu adavomereza nkhaniyi atakambirana. Akadaulo osiyanasiyana akhala akuthirira ndemanga za kufunika kothamangitsa kafukufukuyu kuti dziko la Malawi liyambe kulima nkugulitsa chamba chomwe ena akuti chikhoza kusintha chuma cha dziko lino. Katswiri wina wa bizinesi yokhudza malonda a chamba wa ku Canada wa Green Quest Pharmaceuticals adati chamba chili ndi mtengo wabwino pamsika wa maiko ndipo chikhoza kubweretsa ndalama zambiri mdziko. Chamba chomwe akadaulowa akulimbikitsa ndi chomwe amagwiritsa ntchito mmafakitale popanga zinthu zosiyanasiyana monga mankhwala ndipo akatswiri amati mphamvu zake nzochepa poyerekeza ndi chamba chosuta chija chimazunguza bongo. Polankhula ndi Tamvani, mlembi wa nthawi yoona za mbewu zogwiritsidwa ntchito mmafakitale Industry Crops Association (ICA) Hellen Chabunya adati boma likuyenera kukhala ndi chidwi pa kafukufuku wa ulimi wa chamba kuti dziko lino litukuke. Chongofunika apa nkuwonetsetsa kuti tapanga malamulo ogwira okhudza kayendetsedwe ka ulimi ndi malonda a chambachi. Zina mwa izi nkuwonetsetsa kuti taunikaso malamulo ena okhudza mbeu ngati zimenezi, adatero Chabunya. ",2 "Ogwira Ntchito ku Chipatala cha Zomba Akupitilirabe Kunyanyala Ntchito Ogwira ntchito ku chipatala chachikulu cha boma la Zomba ati apitilirabe kunyanyala ntchito ngakhale kuti boma lawatsimikizira kuti lawawonjezera ndalama zomwe amapempha. Mmodzi mwa anamwinowa yemwe sadafune kudzitchula dzina wauza Radio Maria Malawi kuti iwo achita izi kamba koti ndalama yomwe imakhala ya chipepeso choyika miyoyo yawo pa chiwopsezo yomwe amalandira poyamba ya 1, 800 kwacha idakhalitsa komanso inali yochepa. Iwo atinso anamwinowa sakugwirizana nazo zomwe unduna wa zaumoyo wanena kuti ndalama zimenezi alandira nthawi ya mliri wa Coronavirus yokha. Mwazina iwo ayamikira boma kaamba kowatsimikizira kuti alemba anthu ena owonjezera ogwira ntchito mchipatala pomwe ku chipatala cha Zomba kutumizidwe anthuwa okwana 70. Ndizoona kuti a boma anena kuti pakhala kuwonjezera kwa ndalama zachiwopsezo zomwe timapempha ndipo kukambirana kwathu ndi akuluakulu ena ati zipangizo zafika ndipo padakali pano zilipo koma ife ndondomeko zomwe zilipo pakadali pano za ndalama zachiwopsezo chathu ndi yomwe tisakugwirizana nayo, anatero namwinoyo. ",14 "HRDC Yachita Ziwonetsero Zokwiya ndi Kusankhidwanso kwa Makomishonala Awiri Bungwe la Human Rights Defenders Coalition (HRDC) lero lachita ziwonetsero zosagwirizana ndi kusankhidwanso kwa ma commissioner awiri a bungwe la MEC ndi mtsogoleri wa dziko lino Professor Peter Mutharika. Mu mzinda wa Zomba ziwonetserozi zinayambira ku Chinamwali mpaka ku ofesi ya bwanamkubwa wa bomalo. Ziwonetsero za mmbuyomu zokonzedwa ndi HRDC Polankhula kwa atolankhani atapereka chikalata cha madandaulochi, wapampando wa bungwe la HRDC mchigawo chaku mmawa a Madalitso Banda ati akufuna mtsogoleri wa dziko lino avomereze kuti chisankho chichitike pa 23 June pano, momwe aphungu akunyumba ya malamulo agwirizanirana komanso akufuna kuti ma commissioner awiri a bungwe la MEC omwe ndi Dr. Jean Mathanga, komanso Linda Kunje asagwire ntchito pa chisankho chimenechi, chifukwa choti mabwalo a milandu anawapeza kuti adalephera kugwira bwino ntchito pa chisankho chomwe chidachitika pa 21 May chaka chatha. Polalankhulapo atalandira chikalatacho mmalo mwa bwanamkubwa wa bomalo a Chris Nawata ati chikalatachi achipereka kwa anthu oyenelera ndipo chikafika mmanja mwa mtsogoleri wa dziko lino. Ziwonetsero za mtunduwu zachitikanso mmizinda ya Blantyre, Lilongwe ndi Mzuzu. ",11 " Akupopa zimbudzi pochepetsa matenda Ena zimbudzi zawo zikadzadza amagwetsa ndi kukumba china. Uku ndi kutha malo. Lero zinasintha chifukwa khonsolo ya Blantyre mogwirizana ndi Waste Advisers agwirizana zopopa zimbudzi zomwe zadzadza. Iyitu ndi njira yomwe mbalizi zamvana pofuna kulimbikitsa ukhondo mumzinda wa Blantyre pamene matenda a kolera akugwetsa anthu moti kufika lero anthu 26 amwalira. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Kupatula izi, khonsoloyi ikuyenda khomo lililonse mumzinda wa Blantyre kuphunzitsa anthu zaukhondo ndipo nyumba 10 000 azifikira. Amene akuwongolera ntchitoyi ku bungwe la Waste Advisers, Marcel Chisi, adati kupatula ntchitoyi, amanga zimbudzi 30 mwa zimbudzi 100 mumzindawu kuti ukhondo upite patsogolo. Tisamangonena kuti anthu asakodze paliponse koma tikuyenera kumanga zimbudzi kuti anthu azilowa mmenemo polipira kangachepe, adatero Chisi. Tagwirizana ndi makampani amene akugwira ntchito yopopa komanso kumanga zimbudzi zamakono. Anthu akatipeza, tiwalumikizitsa kwa amene angawathandize. Chimpopa chimodzi chimapopa zinthu zochuluka malita 3 600 ndipo munthu alipira K30 000. Komanso mtengo umasintha malinga ndi kutalika kwa malo amene akapopawo. Wachiwiri woona nkhani za umoyo ku khonsolo ya Blantyre, Samden Seunda adati zonyansazo zikapopedwa azizipititsa ku Chirimba, Soche, Blantyre ndi ku Limbe komwe azikazithira mankhwala. Tili ndi chikonzero kuti zonyasazo tizizithira mankhwala ndipo kutsogolo kuno tizipangira nkhuni zomwe mutha kuphikira, adatero Seunda. ",6 "Kwaya ya Sts Symon and Jude Ithandiza Radio Maria Malawi Kwaya ya Saints Symon and Jude ku Chileka mu parishi ya Lunzu mu arkidayosizi ya Blantyre ya mpingo wa katolika, yati ndi udindo wa aliyense kuthandiza Radio Maria ndi zinthu zosiyanasiyana. Mkhalapampando wa kwayayi, Mayi Florence Chirwa, alankhula izi pambuyo popereka thandizo lawo ku wailesiyi mboma la Mangochi. Mayi Chirwa, ati ngakhale kwayayi si ya anthu ochita bwino, komabe anachiona cha nzeru kuti agawane ndi wailesiyi zochepa zomwe ali nazo, pofuna kuthandizira ntchito yofalitsa uthenga wabwino padziko lonse. Titakhala pansi ngati kwaya tinaona kuti ndi kofunika kuthandiza wayilesiyi popeza imathandiza mpingo wathu mu njira zosiyanasiyana ndipo tathandiza ndi ndalama yokwanira 40 thousand kwacha, anatero mayi Chirwa. Polankhulapo mkulu wowona ntchito zokweza wailesiyi a Martha Mwandira, ayamikira kwayayi kaamba kofika ndi thandizo lawo mu nthawi yoyenera, pomwenso wayilesiyi ikukumana ndi mavuto ambiri a zachuma. Ife ndi othokoza kamba koti kwayayi yagwira ntchito yaikulu yothandiza wayilesiyi ndipo thandizoli ligwira ntchito yoyenera, anatero Mwandira. Iwo apephanso anthu akufuna kwabwino kuti adzithandiza wayilesiyi molowa manja kuti ntchito zake zipite patsogolo maka pa nthawi ino ya Coronavirus pomwe zinthu zambiri zayima. ",13 " Malawi siidalakwe za al-Bashir Mphunzitsi wa za mbiri yakale ku sukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, Pulofesa Chijere Chirwa wati dziko lino silingakhudzidwe mnjira iliyonse pokana kuchititsa msonkhono wa mgwirizano wa maiko a mu Africa. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda adaletsa kuti msonkhanowu usachitikenso mdziko muno chifukwa chokakamizidwa kuti limange mtsogoleri wa dziko la Sudan, Omar Hassan al-Bashir. Mkuluyu wakhala akusakidwa ndi bwalo loona milandu ya upandu padziko lapansi la International Criminal Court (ICC) pamilandu ya upandu. Dziko lino limayembekezereka kuchititsa msonkhanowo kuyambira pa 9 mpaka pa 16 mwezi wa mawa ku Lilongwe. Sabata ziwiri zapitazo, Banda adanenetsa kuti ngati al-Bashir angayerekeze zobwera mdziko muno adzamangidwa. Koma akuluakulu a mgwirizanowo adati Malawi monga dziko lomwe lichititse msonkhanowo likuyenera kulandira munthu aliyense yemwe ndi membala wa mgwirizanowo. Izi zidasokoneza Banda popeza omwe amathandiza dziko lino adanenetsa kuti dziko lino limange al-Bashir akatera mdziko muno. Banda adalengeza kuti sachititsanso msonkhanowo ndipo mmalo mwake msonkhanowo uchitikira mdziko la Ethiopia. Koma Chirwa wati ganizo la Banda lili bwino ndipo silingaike dziko lino pamoto. Ubwino wake nkuti pali maiko ena monga Zambia ndi Botswana omwe ali mumgwirizanowo koma adaneneratu kuti amanga mkuluyu akafika mdziko lawo. Ichi ndichitsimikizo kuti sitidalakwitse chifukwa maiko ena amagwirizana ndi ganizo lathu lomanga mkuluyo, adatero Chirwa. ",11 " Mwambo woika maliro a khanda lozizira Amalawi ngakhale ali ndi miyambo yosiyanasiyana malinga ndi mitundu yawo monga Achewa, Angoni, Atumbuka, Alhomwe, Amanganga, Asena kaya ndi Ayao, koma pamwambo woika khanda lopitirira zochitika zimakhala zofanana. DAILES BANDA adacheza ndi mayi Catherine Ligowe kuti afotokoze mmene mwambo woika khanda lozizira umayendera. Adacheza motere: Ndikudziweni mayi wanga. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Ndine Catherine Ligowe. Ndidabadwa zaka zambiri zapitazo. Ndimachokera ku Ntcheu mmudzi mwa Chikadya, T/A Ganya. Ndili ndi ana asanu ndi awiri. Ndinenso namkungwi kumudzi kwathu komanso ndidali mzamba. Kuno ku Mzuzu mukupezekako bwanji? Mavuto mwanawe. Kuyeseyesa kuti tipezeko koponyako mkamwamu. Ku Mzuzu kunonso ndinu namkungwi? Ayi, ku Mzuzu kuno unamkungwi wanga umakhala wa mmakwalalamu koma kumudzi ndi komwe ndimagwira ntchitoyi kuchinamwali, tere chaka chomwechi ndidali komweko. Mutiuzeko pangono za maliro akhanda lopitirira Inu mufuna mudziwe chani? Tiyambe ndi mwambo wa maliro mmene umakhalira. Khanda lopitirira limatchedwa kuti khanda lozizira chifukwa mayi a khanda lija amakhala kuti sadakhale kaye pamodzi ndi mwamuna. Mukutanthauza kuti khanda litamwalira pamiyezi iwiri makolo ake asadakhalire malo amodzi mwambo wake umakhala ngati wa khanda lopitilira? Eya, chifukwa timakhulupirira kuti mwanayo sadatenthetsedwe ndi bambo ake. Zimayenda bwanji? Mwana uja akamwalira amakaikidwa ndi azimayi okhaokha koma azimayi aja saloledwa kulira malirowo chifukwa kulira kuja kumachititsa kuti mayi uja asadzaberekenso. Manda a malirowa sakhala akuya ngati a maliro a munthu wamkulu. Chifukwa chiyani sakhala akuya? Kalekalelo makolo athu ankakhulupirira kuti manda a khanda lozizira akakhala akuya kwambiri mayi wa khandalo sadzaberekanso. Ndiye maliro a mapasa mumachita bwanji? Akamwalira mmodzi mwa ana amapasa azimayi akalira malirowa timakhulupirira kuti mwana wotsala uja amamwaliranso, komanso tikamaika malirowa timaika khanda lomwaliralo ndi mvunguti pambali pake kuti mzimu wake uziona ngati akadali ndi mnzake uja. Nanga wotsalayo mumatani naye? Ameneyo timamusambitsa mumankhwala kuti mzimu wa mnzake uja usamamubwerere. Tsopano inu mumati mudali mzamba, mudabadwitsako mwana wopitirira? Ayi, palibe mwana wopitirira amene ndidabadwitsako. Mudasiyiranji ntchitoyi? Boma lidaletsa komanso anthu amene amabereketsa azimayi amafa maso nchifukwa chake anamwino ambiri ochiritsa azimayi kuchipatala amakhala ovala magalasi. Kalekalelo mzamba asadayambe kugwira ntchito amayamba kaye wasamba mankhwala kuti adziteteze ku ukhungu. Chimachititsa kufa masoko ndi chiyani? Chimachitika ndi chakuti azimayi akamabereka amachita zinthu zodabwitsa zambiri ndiye ukaona zinthu zimenezo kwanthawi yaitali maso aja amafa, umangoona zinthu mwa mbuu. Zikomo kwambiri chifukwa cha nthawi yanu. Zikomo. ",1 " Za kulephereka kwa zisankho Muzina Edi mwana Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Edi sebe santu Muzina zizata mfana Ya muzina Sindikudziwa ngati Papa Wemba nyimboyo adaimverapo koma ndimo ndinkayimvera pamene inkaphulika malo aja timakonda pa Wenela. Gervazzio ndiye adaika nyimboyo pokumbukira Papa Wemba amene watsikira kwachete. Koma dziko ili! Zoona likutenga anthu ofunika ndi otchuka, achina Prince, kusiya ife ojiya, osolola ndi osenza pano pa Wenela. Imfa ikusiya zilengwalengwa. Tsiku lina ndidzaipha imfa yotenga mayi kusiya mwana akulira. Tsikulo wina adati ndipite ndikaitanire ku Mibawa. Koma nkadadziwa kuti amandikankhira kunkhondo! Padafika asirikali atavala nkhwani-nkhwani. Komatu eni minibasi samaimva, ati khobwe akatolera kuti? Nawo adabwera ndi mapanza awo, inde magigo. Sitiimva. Minibasizi ndi zanu kuti muzitolera ndalama? adatero phanza wina, atanyamula miyala. Kupanda nzeru. Malowa ndi anu? Kodi ogulitsa nkhwani mumsika angamemane kuti azitolera ziphaso ndiwo chifukwa nkhwaniwo ndi wawo? Kupusa! Mnyumba ya mwini saotchera mbewa, adatero wapolisi wina, akukanyanga mmodzi mwa magigowo nkumuponya mchimbaula adachilawa Chihana. Apo ndeu idabuka koma paja lamulo liposa mphamvu, akhonsolo adawina ndipo adayamba kutolera ndalama kuchokera kwa madalaivala. Nditabwerera ku Wenela, ndidapeza Abiti Patuma ndi ena onse akumvetsera wailesi. Chisankho chimati chikhalepo ku Mchinji chalephereka. Boma silidapereke ndalama ati chifukwa lilibe, adatero muulutsi. Boma lilibe ndalama bwanji? Koma chisankho cha ku Zomba ndiye adapeza ndalama? Pafa khoswe apa, adatero Abiti Patuma. Paja nawe, kumangomva fungo la khoswe paliponse? Kulitu njala uku, adatero bambo amene adali naye tsikulo. Zanu. Komabe inetu ndikuona kuti Dizilo Petulo Palibe ikuona kuti kuchititsa chisankho ku Mchinji kukhoza kuchititsa Male Chauvinist Pigs kuoneka mashasha, adayankha Abiti Patuma. Abale anzanga, musandifunse amatanthauzanji chifukwa nane sindikudziwa. Pajatu ine za matchera ayi. Padakalipano boma likuphwanya malamulo omwe amaneneratu kuti chisankho chiyenera kuchitika pasanathe masiku mwakuti, adatero Abiti Patuma. Mukutayatu nthawi. Paja zomatiuza kuti chakuti chichitike pofika tsiku lakuti si mbali yathu, adatero bambo adali naye uja. Mukutanthauza kuti nthawi yokhala pampando ikadzatha, Mustafa sadzafuna kubweza mpando kwa Ajibu? Adangoti duuu mkulu uja. Adalandira foni. Mwati bwanji? Shati Choyamba watisiya? Zabodza izo, nkadamva. Ndikudziwa kuti ali ku Tajkstan komwe amuchotsa dzino dzana. Kukonda kupekera ena imfa bwanji? Akukupanitu makofi akabwera, adatero mkuluyo adatero. Imeneyinso idandipita. Malingaliro adali kwa Papa Wemba komanso Prince. ",11 " Mlandu wa Savala ukupendekeka Mlandu wa mayi wa zaka 33, Caroline Savala, yemwe khothi lidamupeza wolakwa pamlandu wakuba ndalama za boma zokwana K84 miliyoni ukuyenda mwapendapenda. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Savala yemwe amachita bizinesi ya zomangamanga adamupeza wolakwa ndipo akuyembekeza chigamulo cha khothi pa zachilango chake koma Lachisanu lapitali kudali ngati sewero ku bwalo la milandu pomwe womuimira pamlanduwo Ralph Kasambara adalephera kubwera kubwalolo. Sadayankhe funso ngakhale limodzi: Savala (kumanzere) Kusabwera kwa Kasambara mmawa wa Lachisanulo kudakwiyitsa wogamula mlanduwo Fiona Mwale yemwe adaimitsa mlanduwo kuti upitirire 2 koloko masana. Nkhaniyi ipitirira 2 koloko masana ano kuti woimirira mayi Savala abwere ndipo ngati sabwera tikamba nkhani popanda wowaimira,adatero Mwale. Malingana ndi ndondomeko za ku bwalo la milandu, tsiku likakhazikitsidwa ndipo woimirira munthu pamlanduwo walephera kubwera pachifukwa chilichonse, amayenera kudziwitsa bwalo la milandulo nthawi yabwino kapena kutumiza okamuyimirira. Mmawa wa Lachisanu, kalaliki wa kukhotilo adali kalikiliki kuyesetsa kulumikizana ndi Kasambara koma sizimatheke zomwe zidachititsa Mwale kuti asinthe nthawi ya mlandu. Nthawi ya mlandu itafika 2 koloko masana, Kasambara sadaoneke kubwalo la milandulo ndipo mmalo mwake adatumiza womuimirira Tisilira Kaphamtengo, yemwe adapempha wogamulayo kuti mlanduwo awusuntheso poti iye samautsatira bwinobwino. Ine ndiwongoimirira a Kasambala omwe sakumva bwino mthupi koma poti nkhaniyi sindikuyitsata bwinobwino ndimati ndipemphe kuti isinthudwe ndipo idzakambidwe tsiku lina, adapempha Kaphamtengo. Mwale adakana kumva pempholi ponena kuti zomwe adauza khothi Kaphamtengo zokhudza kusamva bwino mthupi kwa Kasambala amayenera kuuza bwalolo nthawi yabwino ndipo adati mlanduwo upitirirebe. Mwale atanena izi, Kaphamtengo adapemphanso kuti alole kuti Savala asayankhe funso lililonse limene afunsidwe poopa kupotoza nkhani ndipo pempholi lidaloledwa. Savala adafunsidwa mafunso 10 koma sadayankhepo ngakhale limodzi mpaka mlanduwo udayimitsidwa. Savala adapezeka wolakwa pa 18 July 2015 wogamula yemwe adalinso Mwale atapeza umboni wakuti mayiyu amalandira ndalama zosagwirira ntchito kuchoka ku unduna wa zokopa alendo. Savala,yemwe samagwira ntchito mboma nthawi yomwe amaganiziridwa kuti amalandira ndalamazo, adauza bwalo la milandu muumboni wake kuti iye adachita kukokeredwa mu kangaude wachinyengowu ndi mkulu wina yemwe amagwira ntchito ku unduna wazokopa alendo Leonard Kalonga komanso mnzake wa ku ubwana Florence Chatuwa omwenso amayimbidwa mlandu omwewo. ",7 " Kudzula: Mpeni wofunikira kwa butchala Popha mbuzi kapena ngombe amagwiritsa ntchito zida zosiyanasiyana monga nkhwangwa, zikwanje ndi mipeni. Umodzi mwa mipeniyi umatchedwa kudzula ndipo eni ake akuti mpeniwu amagwiritsa ntchito posenda nyamayo. STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi Innocent Chimsewu yemwe amapha nkugulitsa nyama ya mbuzi kuti adziwe chinsinsi chosagwiritsa mpeniwu pantchito zina koma kuphera ndi kusendera nyama basi. Iwo adacheza motere: Tandiuze dzina lako ndi ntchito yomwe umapanga, mnyamata. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Dzina langa ndine Innocent Chimsewu ndipo ndimapha mbuzi ndi kumagulitsa nyama yake mumsika wa ku Area 22A ku Lilongwe. Kodi pali zinsinsi zilizonse zokhudzana ndi bizinesi ya nyama makamaka ya mbuzi kapena ngombe? Chimsewu kusenda mbuzi ndi mpeni wa kudzula Ndikudziwa zomwe mukutanthauza ngakhale mukukhala ngati mukukuluwika pangono ndipo yankho lake ndi ili: bizinesi ya nyama ya mbuzi kapena ngombe nchimodzimodzi bizinesi ina iliyonse. Apa ndikutanthauza kuti momwe anthu amayendetsera bizinesi ina iliyonse, ndimoso zimachitikira mbizinesi ya nyama. Ndidamvako kuti mpeni wosendera nyama ya malonda sugwiritsidwa ntchito zina, zimenezi nzoona? Nzoona, mpeni umenewu tikamaliza kusendera mbuzi kapena ngombe timautsuka bwinobwino kuusunga pamalo abwino kuti usamalike. Kunena zoona si kuti pali kugwirizana kulikonse koma kuti anthu amangochita izi ngati njira imodzi yosamalira mpeniwu kuti usasowe. Dzina la kudzula lidabwera bwanji? Ndi dzina basi monga momwe maina ena onse amayambira kapena kubwerera. Ena adangoganiza kuti mpeniwo ukhale kudzula mwina potengera ntchito yomwe umagwira yosendera nyama. Umakhala mpeni wooneka bwanji? Ndi mpeni monga momwe umakhalira mpeni wina uliwonse koma uwu umakhala wakuthwa kwambiri komanso kawirikawiri, umaninga mmphepete imodzi ngati wosokera nsapato kaamba konolanola. Timanola pafupipafupi chifukwa mpeni wobuntha umanyotsola nyama posenda. Mnofu wambiri umatsalira kuchikopa. Ndikubwezere mmbuyo pangono. Mpeni wa kudzula utasowa, mpeni wina uliwonse sungagwire nthito yosendera mbuzi kapena ngombe? Ukhoza kusendera bwinobwino popanda choletsa. Komansotu posenda mbuzi kapena ngombe si kuti pamakhala mpeni umodzi wokha, ayi, kungoti si mipeni yonse yomwe ili kudzula, koma wokhawo womwe ndalongosola uja ndipo umenewu ndiwo suloledwa kugwiritsa ntchito ina iliyonse Ntchito ina ya kudzula ndi chiyani? Kudzula amagwira ntchito zambiri pakupha ndi kusenda mbuzi ndi ngombe. Ntchito yoyambirira ndi yothyolera fupa la pakholingo. Wocheka pakhosi akacheka, pamakhala fupa lomwe limatsalira lomwe limasunga moyo ndiye amatenga kudzula nkuthyolera fupa limeneli. Ntchito ina, poti mpeniwu umakhala wakuthwa kwambiri, ndi kuchekera zammimba monga mtima, chifu, matumbo ndi ndulu. Makamaka pa ndulupo, ukagwiritsa ntchito mpeni wobuntha, mwangozi ukhoza kuthudzula ndulu ndiyetu kungotero, ndiwo yonse yaonongeka. Nanga mubutchala mogulitsira nyamayo kudzula safunika? Si kwenikweni, iye kwake nkophera ndi kusenda koma zikavutitsitsa akhoza kugwira ntchito yochekera mubutchala si kuti china chake chingachitike, ayi, koma kuti ambiri amaumira kutero kuopa kusowetsa. ",15 " Kolera yaluma mano Nthenda ya kolera imene idayamba ngati njerengo mwezi wa November chaka chatha, ikukwererabe moti kuchoka Lachisanu sabata yatha chiwerengero cha anthu odwala nthendayo chidachoka pa 420 kufika pa 459 Lachiwiri. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Malinga ndi zikalata zochokera ku Unduna wa Zaumoyo, anthu 6 amwalira ndi matendawa ndipo anthu 14 akulandira thandizo mmalo apadera amene undunawo udakhazikitsa mmaboma ena. Matendawa akhudza maboma a Karonga, Kasungu, Dowa, Nkhata Bay, Lilongwe, Salima, Mulanje, Nsanje, Chikwawa, Likoma, Rumphi ndi Blantyre. Matendawa adafala ndi msodzi wina, amene adaitenga ku Wiliro mboma la Karonga ndipo adafika nayo ku Ngala, kumene asodzi amafikira ndi kugulitsa nsomba zawo. Msodziyo adafika padokopo ali wefuwefu ndipo adachita chimbudzi mphepete mwa nyanja. Malinga ndi Idah Msiska, yemwe ndi wapampando wa komiti ya chitukuko ya mmudzi mwa Muyereka ku Ngala, matendawa adafala kwambiri chifukwa cha kusowa zimbudzi komanso utchisi wa deralo. Wodwala woyamba adafika pagombe nkuchita chimbudzi ndipo tizilombo tidafalikira mmadzi. Chovuta china nchoti nsomba zimaola kwambiri kumalowa ndipo zimaitana ntchentche zomwe zimafalitsa matendawa. Padakalipano tikuyendera khomo ndi khomo kuti tithane ndi matendawa ndipo amene sakutsatira malangizowa amakumalipa chindapusa, adatero Msiska. Iye adati chodziwikiratu kuti matendawa afala chifukwa ena amachita chimbudzi mnyanja momwe enanso amatunga madzi ogwiritsa ntchito pakhomo. Malinga ndi mmodzi mwa anthu 258 amene apezeka ndi matendawa ku Karonga, Baxter Nyondo, matendawa ndi wovuta ndipo akungoyamika Mulungu kuti akadali moyo. Iye Lachiwiri tidamupeza akulandira thandizo pachipatala chachingono cha Ngala. Sindinkadziwa chinkandichitikira. Ndinkangothulula osalekeza. Pano bola. Ndikuyamika chifukwa achifundo adanditengera kuchipatala msanga, adatero iye. Iyi ndi nkhani yolingana ndi yomwe adatambasula Mercy Kachepa yemwe ankadikirira mbale wake pamalo a padera a odwala kolera ku Bwaila ku Lilongwe. Adafika kunyumba kuchoka kosewera akudandaula mmimba. Posakhalitsa adayamba kugudubuka, uku akudziyipitsira. Kupanda kuikapo mtima akadapita, adatero Kachepa. Lolemba Nduna ya za Umoyo Atupele Muluzi idakayendera malowo komwe adatsimikiza kuti zinthu zaipa. Nkhondo ndiye ikumenyedwa kuti vutoli lithe koma kunena zoona, matendawa atikakamira ndipo liwiro lomwe akufalira likuopsa kwambiri, adatero iye. Muluzi adauza Nyumba ya Malamulo sabata yatha kuti katemera wa kolera yemwe boma likupereka akhoza kuthandiza kuthetsa kufala kwa matendawa ataperekedwa mmadera ambiri makamaka omwe ali pachiopsezo. Oyanganira ntchito za umoyo mmaboma a Lilongwe ndi Karonga kumene kolera yafala kwambiri, adati sakugona tulo kaamba ka matendawa. Woyanganira ntchito za umoyo mboma la Lilongwe, Alinafe Mbewe, adati vutoli lakula kwambiri kwa Mitengo ku Area 36 ndi Kauma komwe anthu ambiri omwe apezeka ndi matendawa amachokera. Zinthu sizikusintha kwenikweni koma tikuyesetsabe. Kuchoka pa 28 December, 2017 kudzafika pa 23 January, 2018, anthu 35 ndiwo adapezeka ndi kolera koma kuchoka pa 24 January kudzafika pa 12 February, anthu 82 ndiwo apezeka, adatero Mbewe. Ndipo Dr Phinias Mfune ku Karonga wati vutoli likukula chifukwa tsiku lililonse pakupezeka munthu mmodzi wotenga nthendayi. ",6 " Apha mkazi ndi apongozi kaamba kothetsa banja Mnyamata wina wa ku Mangochi wagwa mmanja mwa apolisi atapha mkazi ndi apongozi ake kaamba kothetsa banja. Stephen Sani wa zaka 25 adavomera mlandu wopha mkazi wake Annie Smoke ndi apongozi ake, Enifa Smoke, ndipo pomwe timasindikiza nkhaniyi nkuti iye akuyembekezera kukaonekera ku khoti. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Sani adati adachita zaupanduzo kaamba koti makolo a mtsikanayo adathetsa banja lake ndi cholinga choti akapitirize maphunziro. Mayi ndi gogo wa ophendwawo, Alida Moyenda, adati awiriwo adalowa mbanja atachimwitsana. Panthawiyo nkuti Annie ali ndi zaka 16, komanso ali folomu 1. Gogo Moyenda adati poona kuti mtsikanayo adali wamngono, komanso wanzeru kwambiri pamaphunziro adaganiza zomubwezera kusukulu, koma mwamunayo adakana. Timafuna Annie apitirize maphunziro, koma popeza mwamunayo amakana tidangoganiza zothetsa banja kuti pasakhale kupingana kulikonse, adatero gogoyu. Iye adati banja la awiriwo lidatha pa August 5 2017 ndipo mtsikanayo adakayambiranso sukulu. Gogoyu adati banja la Sani ndi Annie mudalibe mavuto ena aliwonse, koma chomwe makolowo amafuna ndi choti mkaziyo aphunzire. Padalibe mavuto ena aliwonse, koma chomwe chimatikhudza nchoti mtsikanayo adali wangono woyenera kukhala pasukulu osati pabanja, adatero Moyenda. Mneneri wa polisi wa mboma la Mangochi, Amina Tepani Daudi, adati pa August 13 2017 Annie ndi amayi ake adatengana ulendo wokaona mbale wawo wina mmudzi mwa Mbapi mboma lomwelo. Popeza mwamunayo amakhala moyandikana ndi makolo amtsikanayo, adadziwa za ulendowo ndipo adawatsatira mpaka pa famu ya Funwe pomwe adawaimitsa ndi kuwachita chiwembu. Titalandira uthenga woti mu famu ya Funwe mwapezeka mitembo iwiri, tidaitengera ku chipatala chachingono cha Monkey Bay komwe adatiuza kuti anthuwo adamwalira kaamba ka kutaya magazi kwambiri atabaidwa ndi mipeni pakhosi, adatero Daudi. Iye adati apolisi adagwira Sani pomuganizira kuti ndiye adachita zaupanduzo. Atamufunsa, adavomera mlanduwo moti akuyembekezera kuyankha mlandu wakupha womwe ukutsutsana ndi ndime 209 ya malamulo a dziko lino. Akapezeka wolakwa, Sani akagwira ndende moyo wake wonse. Mkazi wa mtsogoleri wa dziko lino, Gertrude Mutharika, wakhala akulimbikitsa atsikana omwe adalowa mbanja akadali a angono kuti abwerere kusukulu. Malingana ndi kafukufuku wa mabungwe osiyanasiyana kuphatikizirapo la UNDP, atsikana ambiri mdziko muno amalowa mbanja asadafike zaka 18. Mkulu wa bungwelo, Dan Odallo, adati vutoli ndi lomwe likuchititsa kuti atsikana ambiri azisiira panjira sukulu. Pafupifupi theka la atsikana a mdziko muna amalowa mbanja asadafike zaka 18, adatero Odallo. Pofuna kuthana ndi vutoli, Nyumba ya Malamulo idakhazikitsa malamulo woti atsikana azilowa mbanja akakwana zaka 18 kapena kupotsera apo. ",7 "Usi Wapempha Amalawi Alemekeze Mutharika Pomuchotsa pa Mpando Wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha UTM, Dr. Micheal Usi walangiza anthu mdziko muno kuti akavote pa chisankho chikudzachi ndi cholinga chochotsa President Peter Mutharika pampando. Dr. Usi amalankhula izi mboma la Mangochi pamene amalandira a Yusuf Kusweje omwe anayimira ngati phungu mchipani cha UDF mdera lapakati mboma la Mangochi yemwenso anali wachiwiri kwa mkulu wokopa anthu mchipanichi yemwe tsopano walowa chipani cha UTM ndi akuluakulu ena asanu ochokeranso ku UDF. Dr. Usi ati ulemu waukulu umene amalawi angapereke kwa President Mutharika ndi kukavota kuti asakhalenso mtsogoleri wa dziko lino ndipo azipuma. Pamenepa iwo ati kulowa kwa anthu mchipanichi kukuwonetsa poyera chikhulupiliro chomwe ali nacho mu utsogoleri wa Dr. Saulos Chilima. Tachilandira bwino kwambiri ndipo chilichonse chimayangana mtsogoleri ndipo mmene zakhaliramu zasonyeza kuti anthu ayamba kuzindikira, anatero Usi. Polankhulapo a Yusuf Kusweje ati achita kampeni yamphamvu mboma la Mangochi ndi cholinga chakuti mgwirizano wa UTM ndi MCP upeze mavoti ochuluka mbomalo. ",11 "Apempha Boma Liyike Chidwi Mzipata za Mdziko Muno Mmodzi mwa anthu omwe amatsatira bwino nkhani zochitika mdziko muno a Coxley Kamange apempha boma kuti liyike chidwi chake pa zipata zolowera ndi kutulukira mdziko muno pofuna kuti nthenda ya COVID-19 isapitilire kufalikira mdziko muno. Zipata za dziko lino zidakali zotsekula A Kamange amalankhula izi mu mzinda wa Blantyre pothilirapo ndemanga pa momwe boma likugwilira ntchito yolimbana ndi kufala kwa kachilombo komwe kakuyambitsa nthendayi ka Corona-virus mdziko muno. Tati tipemphe ku boma kuti mmaboda mukhale chitetezo chokwanira poyika malo oti anthu obwera kuchokera ku maiko a kunja azisungidwa kumeneko kufikira masiku omwe achipatala akunena, anatero a Kamange. Iwo anapemphaso boma kuti liyike nthawi zapadera zosiyana mmisika pofuna kuchepetsa chiwerengero cha anthu opezeka mmisikayi. ",14 " Milandu mbweee! mu 2016 Chapita chaka cha 2016 chomwe dziko lino lidaona ina mwa milandu ikuluikulu ikulowa mmabwalo a milandu ndi kuweruzidwa. Umodzi mwa milanduyi udali wa yemwe adali nduna ya za chilungamo zaka zapitazo yemwenso ndi kadaulo pa malamulo, Ralph Kasambara. Kasambara, pamodzi ndi Pika Manondo komanso MacDonald Kumwembe adayankha mlandu woti adakonza chiwembu chofuna kupha mkulu woyendetsa ndondomeko za chuma wakale Paul Mphwiyo mu 2013. Kasambara (wasuti) kupita kundende Mwezi wa July, bwalo la milandu lalikulu mumzinda wa Lilongwe lidamupeza Kasambara wolakwa pamlanduwo ndipo mwezi wa August adagamulidwa kukasewenza jere kwa zaka 13. Manondo ndi Kumwembe adagamulidwa kukasewenza jere zaka 15 ndi 11 aliyense pa milandu iwiri: yochita upo pofuna kupha komanso mlandu wofuna kupha Mphwiyo panja pa nyumba yake ku Area 43 mumzinda wa Lilongwe usiku wa September 13 chaka cha 2013. Milanduyi asewenza paderapadera. Pamodzi, Mandondo ndi Kumwembe asewenza zaka 26. Mlanduwutu tsopano uli kubwalo la apilo. Mchakachi tidaonanso fisi wa ku Nsanje, Eric Aniva, akukalowa mchitokosi pogona ndi amayi 104 mbomali. Aniva yemwe ndi wa zaka 45, wochokera mmudzi mwa Tosina kwa mfumu yaikulu Mbenje, mbomalo adapezeka wolakwa pa milandu iwiri yokhudza kuika miyoyo ya ena pachiswe potsatira miyambo ya makolo. Aniva adanjatidwa pomwe adauza wailesi ya atolankhani a British Broadcasting Corporation (BBC) za ufisiwu mwezi wa July. Ngakhale Aniva adaukana mlanduwu pa November 22, woweluza milandu Innocent Nebi adamugamula kukasewenza zaka ziwiri ku ndende. Padakali pano, womuyimira Michael Goba Chipeta wachita apilu. Nawo mlandu wa mtsogoleri wagulu lomenyera ufulu wolanda malo mmaboma a Thyolo ndi Mulanje la Peoples Land Organisation (PLO) Vincent wandale udali mkamwamkamwa mwa anthu mchakachi. ",7 "Anatchezera Akufuna mwana Zikomo Gogo, Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Banja ndi mwamuna wanga lidatha mu 2011. Ndidapeza mwamuna wina yemwe timamvana ndipo tidakayezetsa komwe adatipeza kuti tilibe kachilombo koyambitsa Edzi.Vuto ndi lakuti bwenzi langalo limakonda zogonana komanso limandiletsa kuchita za kulera. Wina adandiuza kuti bwenzi langalo lili ndi mkazi koma nditamufunsa adakana. Tsiku lina ndidaimba foni 5 koloko mbandakucha ndipo ndidamva kulira kwa mwana wa khanda. Nditamufunsa adakana ndipo adati ndi wa khomo loyandikana nalo. Ndizimukondabe? R, Chiradzulu Wokondeka R, Mwakumana ndi chilombo cha bodza. Wakunamizani kuti akufuna mwana chonsecho pansi pamtima akudziwa kuti akakupatsani mwana adzakuthawani nkupitiriza kukhala ndi mkazi wake. Wakunamizaninso kuti mwana amalira ndi woyandikana nawo nyumba. Ngati zili zoona, bwanji adadula foni? Asakutayitseni nthawi ameneyo. ",15 " Za maukwati, mabanja Money is gooooood Musayense njerego, awa ndi mawu ochokera munyimbo ya Miracle Money ya mnyamata wodziwa kuimba nyimbo zauzimu, Onesmus. Poyamba, ndinkamva ngati akuti God is good! Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Iyitu ndi nyimbo yauzimu imene imakamba za ndalama zozizwitsa zimene zingapezeke mkachikwama kanu kapena kubanki modabwitsa. Akhoza kukhala mamiliyoni. Si za kashigetitu! Major do it! Major do it! Pamenepanso ndimayesa akuti God do it! God do it! Zoona, ambiri timalambira dzuwa mmalo molambira wolenga dzuwalo. Musayambe kundinena kuti ine zindikhudza bwanji. Inetu ndimakhulupirira kwambiri Mateyu 7 vesi ya 1: Osaweruza ena chifukwa ndi mlingo umene uweruzira ena, nawenso udzaweruzidwa. Ndine ndani ine, kapunthabuye, kafucheche, kwakwananda ndipo ndikadakhala nsalu bwenzi ndili kilimpulini. Sindinakumalizireni nkhani ija sabata yatha. Tidaika zovuta kumanda ena pafupi ndi pa Wenela. Ubwino wake, wotisiyayo adali atagula kale puloti yake kumasanoko. Titaika zovutazo, mkulu wina adanditengera pambali: Tade kodi panthumbira paja anaikapo maluwa chifukwa chiyani? Kodi malemuwo adali kalipentala? Nanganso anaikapo mtanda wa thabwa, kodi malemuwo adali kalipentala? Sindikaika kutsogoloku adzawaka mandawo ndi simenti ndi quary ngati malemuyo anali kontilakita. Sindidamuyankhe. Titafika malo aja timakonda pa Wenela, kudatulukira mkulu wina atanyamula zibonga ndi mikondo. Tiwaphe basi! Amenewa aphedwe basi! Ndithu pa filling station munthu angathire mafuta kotulukira utsi? adafunsa mkulu wa zikwanjeyo. Dzina lake ndi Nike Masonda, mnzake wa Adona Hilida ku Polisi Palibe. Tsono akadati alowe kumpanda ku Sanjika bwenzi ataika malamulo wotani mkuluyo? Zidandipita. Koma Abiti Patuma akuoneka kuti adazitolera. Pezani zina zokamba. Ndimayesa muzinena za chimbudzi choyendayenda cha Moya Pete. Zomwe mukunenazo tidazimva kale. Ati Mugabe adawauza akwatirane ndipo mubadwe mwana, apo ayi awakhiya pakhosi, adatero. Ndipo izo zili apo, tidamvaponso za wina amene ankanena kuti satana akadakhala wa maganizo otere bwenzi atapusitsa Adam osati Hava kuti adye chipatso cha pakati pamunda. Koma zochitika kuchipinda kwa wina inu zimakukhudzani chiyani? adafunsa Abiti Patuma. Mkulu uja adati: Musathe mpweya, malamulo amaletsa kuchita zosayenerazi. Ngakhale malembo oyera amaneneratu. Malamulowo amaneneratu kuti si bwino kugonana motsutsana ndi chilengedwe. Titati tilowe mzipinda mwa inu mukudzitcha olungama sitikapeza mukuphwanya lamulo? adaphaphalitsa funso Abiti Patuma. Abale anzanga, mwinatu mukufuna kumva maganizo anga pankhaniyi. Ndine mmodzi mwa anthu amene amakhulupirira kuti ngakhale nyerere zimadziwana kuti iyi ndi yaimuna, iyo yaikazi, chimodzimodzi agalu, abakha, nguluwe ndi akamba. Chinanso nchakuti tikadati tonse tiziganiza chomwechi, bwenzi dziko ndi anthu ake alipo? Koma mbali inayi, zochitika kuchipinda kwa ena ine sizindikhudza; ndilibe nazo ntchito. Pamene ena akuchita kusaweruzika ine sindikhala nazo ntchito. Zonse zili apo, ndimakhulupirira kuti chilengedwe chiyenera kutsatidwa basi. Ndimaopa kuti zipata zitatsegulidwa, mwana wanga Zeno akhoza kuona ngati kukhalira limodzi atambala okhaokha palibe chachilendo. ",15 "Zikhulupiliro Zikukolezera Milandu Yogwililira ku Ntchisi Zikhulupiliro akuti ndi zimene zikukolezera kuchuluka kwa milandu yogwililira mboma la Ntchisi. Kaponda: Ena amawona ngati akhwima Wofalitsa nkhani za apolisi mbomalo Richard Kaponda wauza Radio Maria Malawi kuti pali anthu ena omwe amaganiza kuti akagona ndi mwana wachichepere achira ku matenda a edzi, komanso ena amatenga zizimba zochitira bizinesi. Komabe Kaponda wati kudzera mu ntchito yawo yozindikirtsa anthu za kuyipa kwa mchitidwewu, milanduyi yatsikirapo mmiyezi itatu yapitayi poyerekeza ndi miyezi ngati yomweyi chaka chatha. Malinga ndi Kaponda, bomalo linalandira milandu yogwililira 15 mmiyezi ya January mpaka April 2019 ndipo mchaka cha 2020 bomalo lalandira milandu ya mtunduwu yokwana 13. ",14 "Anthu Osadziwika Avulaza ma Monita a Chipani cha UTM ku Mulanje Anthu ena omwe sakudziwika avulaza mamonitor a chipani cha UTM pa malo ena ochitira kalembera wa chisankho mdera la kumwera kwa boma la Mulanje. Anathawitsidwa ndi apolisi-Kaliati Malinga ndi ofalitsa nkhani za apolisi mbomalo Gresham Ngwira, anthuwa atavulazidwa anapita ku polisi kukadandaula ndipo akuluakulu ena a chipanichi omwe ndi a Patricai Kalioati komanso a Bon Kalindo anafikanso ku polisiko kuti akamve mmene zakhalira. Koma anthu ena akuti anayamba kuwowoza akuluakuluwa komanso kuwatsekera njira zomwe zinachititsa kuti apolisi aponye utsi wokhetsa msonzi ndi kubalalitsa anthuwo Anthu ena omwe ndima monitors achipani cha UTM avulazidwa pa malo olembetsera kalembera wa chisankho ndi anthu omwe sakuziwika ndipo atsogoleri awo anafika ku polisi kuti adzawaone koma posakhalitsa kunabwera gulu la anthu ena lomwe linayamba kuwawowoza atsogoleriwo, anatero Ngwira. ",11 "Papa Wapempha Akhristu Athandize Anthu Ovutika Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco wati kusamalira anthu ovutika komanso okalamba ndi njira yokhayo yoonetsa kuti akhristu mu mpingowu amaopa Mulungu. Papa Francisko Papa amayankhula izi pa mwambo wa misa yomwe watsogolera ku likulu la mpingo-wu ku Vatican. Iye wati panthawi ino pomwe anthu ambiri akunva zowawa kumanso kuvutika kamatenda a COVID-19 akhristu akuyeneranso kumadzipereka pothandiza ndi kusamalira anthu ovutika ndikupitiliza kutetedza anthu okalamba. Kumbari ya mantha omwe adza kamba ka matenda a COVID-19 ndi zina zopinga Papa Franciso wati anthu omwe amakhulupilira Mulungu sakuyenera kuchedwa ndi kuchita mantha koma kupempha mulungu kuti awachotsere zovuta zomwe zawagwira pakati pawo. ",14 " Boma likukhazikitsa misika ya zakudimba Boma lili mkati momanga malo ogulitsira zokolola zakudimba ngati njira imodzi yochulukitsira phindu lomwe alimi amapeza pogulitsa zokolola zochokera mu ulimi wamthirira. Ntchitoyi ndi gawo limodzi la ntchito yotukula ulimi wamthirira pokonzanso masikimu 11 mchigawo cha zaulimi cha Blantyre Agricultural Development Division (ADD). Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mkulu woyanganira ntchito yotukula zipangizo za ulimi wamthirira, Cosmos Luwanda wati misikayi, yomwe ilipo 6, imangidwa ku Neno ndi kuchigwa cha mtsinje wa Shire. Iye wati ntchitoyi, yomwe ikugwirika ndi thandizo la ndalama zokwana 12 biliyoni kwacha kuchokera ku African Development Bank (ADB), imanga manthu wa misika mumzinda wa Lilongwe komwe kutakhale zipangizo zapamwamba zotha kusungira ndiwo zamasamba ndi zipatso kwanthawi yaitali. Cholinga cha misikayi ndi kulumikiza alimi ndi ogula mosavuta, adatero Luwanda. Mkulu woyanganira ntchito yomanga msika wa zokolola za kudimba wa Chikwawa, Khama Kammwamba, adati malowa adzakhala ndi malo osungira zokolola, malo otsukira zokolola, magetsi, madzi apampopi ndi zimbudzi zamakono. Misikayi izidzagulitsa zokolola mwachipiku kwa amalonda ochokera kutali. Adindo oyendetsa masikimu ndi amene azidzayendetsa misika imeneyi, adatero Kammwamba. Padakalipano ntchito yokonza masikimu amene ali mupolojeikiti imeneyi ili mkati ndipo masikimuwa akuyembekezeka kuyamba kugwira ntchito yawo usanafike mwezi wa June chaka chamawa. ",4 "Abwenzi Ayamikira Dongosolo la Mariatona Wolemba Richard Makombe Abwenzi a Radio Maria Malawi ati ndi okhutira ndi momwe nyengo ya Mariatona yayendera chaka chino. Mariatona ndi nyengo imene Radio Maria imakonza chaka chilichonse pofuna kupeza thandizo loyendetsera ntchito za wayilesiyi komanso kubwenza ngongole zomwe wayilesiyi ili nazo. Ena mwa abwenzi a wailesiyi ku mwambo wotsekera Mariatona ku Dedza Wapampando wa Abwenzi a Radio Maria mu dayosizi ya Blantyre a James Ngombe awuza Radio Maria Malawi kuti kuyambira pomwe Mariatona inayamba mwezi wa May akhala akutsatira bwino mwa chidwi ndipo ndi osangalala kuti zinthu zayenda bwino mpaka kufikira kumapeto pomwe nyengo ya Mariatona yatsekedwa. A Ngomba ati ngakhale panali zovuta zina monga kusowa kwa mabuku olembapo mmene munthu waperekera thandizo lake anthu ambiri ayesetsa kuthandiza wayilesiyi. Ndipemphe kwa akuluakulu kuti ayesetse kuti mabuku olemberapo maina a anthu omwe apereka thandizo lawo ku wayilesiyi azifikira anthu aku midzi komwe nawo azithandiza wayilesiyi, anatero a Ngomba. A Ngomba apempha akhristu komanso antu kuti apitilize kuthandiza wayilesiyi ngakhale Mariatona yatsekedwa pa 27 July 2019. Poyankhulapo wapa mpando wa Abwenzi a Radio Maria mu dayosizi ya Dedza mayi Elina Tcheza wati iwo ndiokondwa kuti zomwe anakonza kuti zichitike potsekera Mariatona zachitika ndipo zayenda bwino. Ndithokoze onse omwe anatengapo mbali poonesetsa kuti Mariatona wa chaka chino akhale wapamwambaanatero a Tcheza. A Tcheza ati ngakhale panali zovuta zina komabe zambiri zayenda bwino Kamba koti anthu ambiri athandiza ndi katundu osiyansiyana. Mariatona inatsegulidwa pa 4 May ku Zomba Cathedral ndipo yatskedwa ku Mtendere Parish mu dayosizi ya Dedza. ",13 "Galu kusaka mbuyake Nkhani ya agogo anayi amene adaphedwa ku Neno kaamba koganiziridwa kuti adapha munthu mmatsenga idakhudza Amalawi ambiri. Zoona, ngakhale mkulu wa apolisi Lexten Kachama amene Lachitatu adapita komweko kukalangiza anthu za milandu yokhudza ufiti. Chomwe chidapatsa ena chidwi ndi galu ali apayu amene amaoneka kuti amasakasaka mbuye wake. Galuyo adalowa mgulu la anthu nkubwerera osapeza mbuye wakeyo. Kapena naye amangofuna kumva nawo uthenga wa ufitiwo?",15 " Ulimi wamthirira usangokhala nyimbo Mkonzi, Ndimamva chisoni njala ikamagwa mdziko muno chifukwa choti mwagwa chilala pamene tili ndi nyanja ndi mitsinje yambiri yomwe simaphwera nthawi yachilimwe, zomwe zingatithandize paulimi wamthirira. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mthirira ungatipulumutse Kodi, Amalawi anzanga, ndi zoona tizifa ndi ludzu mwendo uli mmadzi? Ndithudi maiko a anzathu amene sadadalitsidwe ndi nyanja ndi mitsinje ngati ku Malawi kuno amaseka chikhakhali akationa tikupempha chakudya kumaiko ena chonsecho tili ndi kuthekera kopeza chakudya chokwanira chaka ndi chaka choti chikhoza kudyetsa fuko la Malawi chaka chathunthu popanda vuto lililonse. Vuto ndi boma lathu lomwe limatsogoza ndale kuposa chitukuko cha dziko ndi miyoyo ya anthu ake. Ndi liti lija adayamba za kulimbikitsa ulimi wamthirira pofuna kuthetsa vuto la njala mdziko muno? Tonse tikudziwa bwino za nkhambakamwa ya Green Belt Initiative. Ndani lero angandilozere kuti Green Belt ili apa? Tidamva zoti boma lagula mathirakitala kuchokera ku India kuti athe kuthandiza alimi mmidzimu pachitukuko cha ulimi. Ali kuti ndipo akuchita nawo chiyani pano? Kugula chakudya kumaiko akunja pofuna kudyetsa fuko la Malawi kuli apo, ndi bwino koposa kuti boma likhazikitse mfundo zolimbikitsa ulimi wamthirira mmbali mwa nyanja ya Malawi ndi kuchigwa cha Shire komanso mmbali mwa mitsinje ina monga North ndi South Rukuru, Runyina, Limphasa kuchigawo cha kumpoto; mitsinje ya Linthipe, Lilongwe ndi Bua mchigawo cha pakati; mitsinje ya Thutchira ndi Ruo kummwera mongotchurapo malo ochepa. ",2 " Apolisi alandira uphungu paziphuphu Bungwe lolimbana ndi mchitidwe wa ziphuphu ndi katangale la Anti-Corruption Bureau (ACB) laphunzitsa apolisi a mumzinda wa Mzuzu za momwe angapewere mchitidwewu. Malingana ndi kafukufuku yemwe lidachita bungwe la Centre for Social Research mu 2013 nthambi ya polisi ya Road Traffic and Safety Services lidapezeka kuti ndiyo ili patsogolo polandira ziphuphu komanso kuchita za katangale mdziko muno. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Kafukufukuyo adapezanso kuti nthambi ya Road Traffic Commission nayo ili patsogolo kuchita mchitidwewu. Mmodzi mwa akuluakulu olimbana ndi mchitidwewu kubungwe la ACB, Patrick Mogha, adati iwo adachiona chofunika kuti awaphunzitse apolisi komanso anthu a madera ozungulira pankhani za ziphuphu kuti athandize kuchepetsa mchitidwewu. Tidaona kuti ndi chinthu chanzeru kuti tiwaphunzitse a polisi za momwe angapewere kapena kudziteteza kumchitidwe wakatangale ndi ziphuphu. Tidazindikira kuti anthu ena pochita mchitidwewu sadziwa kuti akulakwira malamulo komanso akubwezeretsa chitukuko cha dziko mmbuyo, adatero Mogha. Mogha adaonjeza kuti iwo ali ndi chikhulupiriro kuti akaphunzitsa apolisi zithandiza kuchepetsa mchitidwewu. Wachiwiri kwa komishonala wa polisi, yemwenso ndi mkulu wa nthambi yoonetsetsa kuti apolisi akuchita zinthu moyenera (Professional Standards Unit), Esther Wandale, adati iwo ali ndi cholinga chothana ndi mchitidwe wa katangale ndi ziphuphu pakati pa apolisi ndipo ati ali ndi chikhulupiliro kuti zinthu zisintha. Cholinga chathu ndi kulimbikitsa apolisi athu kuti azikhala otsata malamulo komanso odalirika. Izi ndi zikhoza kutheka pokhapokha iwo akudziwa kuti katangale ndi chiyani kwenikweni, adatero Wandale. Mmodzi mwa oyendetsa galimoto zahayala (taxi), Happy Soko, adati akuona kuti maphunzirowa athandiza kuchepetsa mchitidwe wa ziphuphu ndi katangale pamsewu. Iye idadati apolisi ndi omwe amathandiza kulimbikitsa mchitidwewu pamsewu chifukwa akadakhala kuti amatsatira malamulo moyenera si bwezi oyendetsa galimowo akuchita mchitidwewu. Maphunzirowa athandiza koma ndikuona kuti akadaphatikizanso anthu ngati ife zikadathandiza kuthana ndi vutoli mwachangu, adatero Soko. ",7 "Atsikana Osiyira Sukulu Panjira Akuchulukira ku Ntcheu Ofesi yoona za maphunziro mboma la Ntcheu yalimbikitsa atsikana kuti azipitiriza maphunziro awo pofuna kuti atsikana akhale ozidalira pa nkhani za maphunziro mdziko muno. Mlangizi wazamaphunziro mbomali mu zone ya Bunyenga a Sidney Makwecha anena izi pambuyo pa ulendo wao wokayendera maofesi a boma la Ntcheu ndi atsikana ochokera pa school ya Saiwa komwe ndi dera lomwe lili ndi atsikana ochuluka osiyira sukulu panjira mbomalo. A Makwecha ati atsikana ambiri sakupitiriza maphunziro awo kaamba kopatsidwa pathupi zomwe zinachititsa kuti ofesiyi pamodzi ndi amayi ogwira ntchito zosiyanasiyana atsikanawa akazionere okha mmaofesiwa mmene amayi akugwirira ntchito zawo kuti atengerepo chitsanzo pa amayiwa. Taona kuti atsikana ambiri mderali akumasiyira sukulu panjira nde tinawatengera ku boma la ntcheu kuti akakumane ndi amayi anachita bwino pa maphunziro ndipo akuwoneka kuti pamapeto pa ulendowu anawa aphunzirapo kanthu, anatero a Makwecha. Sukulu ya Saiwa ili ku dera la kumudzi ndipo ana ambiri amasiyira sukulu panjira kaamba ka moyo otengera makhalidwe achitawoni zomwe zikumachititsa kuti anawa azitenga pathupi adakali aangono. ",3 " Anatchezera Chikondi amatero? Agogo, Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndine mtsikana wa zaka 20 ndipo ndili kukoleji. Ndili ndi chibwenzi chomwe tidagwirizana kuti tidzamange banja mtsogolo muno. Mnzangayu amati akufuna kuti adzandidziwire mbanja chifukwa akayamba kundigona panopa atha nane filimu. Ndiye akuti poti iyeyu ndi munthu pena zimavuta ndiye akuti akufuna apeze mkazi woti azigonana naye popewa kugonana ndi ine kuti inyeyo adzandikwatire. Kodi kumeneku ndi kukonda? Ndithandizeni, agogo, nditani. Ndine L, Lilongwe Wokondeka L, Bwenzi lakolo ndi munthu wachilungamo, inde, koma chilungamo chake chaonjeza. Munthu wotere osamukhulupirira chifukwa ndi kamberembere. Iyeyu wanena chinthu chanzeru kwambiri kuti pakalipano musamagonane chofukwa akuopa kuti akatero atha nawe chilakolako chifukwa wakudziwa. Koma akuti akufuna apeze mkazi wina wapambali kuti azikapumirako poti iye ndi munthu, nanga iwe wakuuza kuti nawe utha kupeza wina woti uzicheza naye pamene mukudikira kuti mudzakwatirane? Akunama ameneyo; akufuna kuti azioneka ngati munthu wokhulupirika pomwe ndi wachimasomaso ndi akazi ena. Tikamati kudzisunga ndi nonse awiri, osati wina aziti mnzangawe udzisunge koma ine ndikayendayenda. Kunjaku kwaopsatu, ndiye wina azipanga dala zachibwana ngati zimene akunenazo, si zoona ayi. Ngati ndi wachilungamo, iyenso ayenera kupirira kuchilakolako cha thupi kufikira tsiku lomwe mudzalowe mbanja. Koma ngati adayamba kale zogonana ndi akazi ena, mchitidwe umenewo sadzausiya. Ndiye, kunena zoona, mwamunayo sali woyenerera kumanga naye banja chifukwa alibe chikondi chenicheni ndi iwe. Amati mbuzi ikalawa mchere sigwirika! Safuna zoyezetsa Anatchereza, Ndakhala ndili pachibwenzi ndi mtsikana wina kwa chaka chimodzi ndipo timakondana kwambiri. Ndine Mkhristu ndipo ndikhulupirira kuti sibwino kumagonana ndi wachikondi wako musadalowe mbanja lomanga. Ndakhala ndikumva malangizo oti masiku ano ndi bwino kukayezetsa magazi musanaganize zolowana, koma mnzangayu nditamuuza zimenezi adati ine zimenezo ndiye ayi. Kumufunsa chifukwa chake adati ineyo ngati ndikudzikaikira ndipite ndikayezetse, osati iyeyo. Akuopa chiyani? MJ Lilongwe Odi MJ, Akuopadi chiyani ameneyo? Pati bii, pali munga, ife akale timatero. Chilipo chimene akuopa chifukwa akanakhala kuti ali bwinobwino, si bwenzi akuchita kukanira patalitali kuti ine toto, pita wekha. Kudziwa mmene munthu ulili usanalowe mbanja ndi chinthu chabwino kwambiri, makamaka masiku ano pamene kuli mliri wa kachilombo ka HIV/Aids. Mundimvetse bwinobwino pamenepa: si kuti munthu akapezeka ndi HIV ndiye kuti sayenera kukwatira kapena kukwatiwa, ayi. Munthu aliyense ali ndi ufulu wokhala pabanja, koma zimakhala bwino kudziwa mmene mthupi mwako mulili pofuna kukonza tsogolo la banja lanu. Ngati wina apezeka ndi kachilombo kapena matenda ena kumphasa mumadziwa chochita pofuna kudziteteza kuti nonse mukhale moyo wathanzi. Komanso ngati mukufuna mwana mbanja mwanu madotolo amadziwa njira zokuthandizirani kuti mwana wanu asatenge nawo kachilomboko. Chachikulu ndi chikondi pakati panu-pali chikondi palibe mantha. Mufotokozereni wokondedwa wanuyo zimenezi kuti amvetsetse, koma ngati akumenyetsa nkhwangwa pamwala, musiyeni ameneyo, muyangane wina amene angakumvetsetseni pankhani yoyezetsa magazi. Nsalu ya lekaleka Anatchereza, Ine ndi mwamuna wanga takhala pabanja zaka ziwiri ndipo nthawi yonseyi takhala tikugwiritsa ntchito njira zolera chifukwa mwamuna wanga amati nthawi yoti tikhale ndi mwana sinakwane-titoleretolere kaye kuti tisadzavutike tikadzakhala ndi mphatso ya mwana mnyumba mwathu. Kunena zoona zimene amati titoleretolere kaye sindikuziona, komanso anthu kunjaku ndiye akumatiseka ndi kumatinyogodola kuti sitibereka. Ine ndiye ndatopa nazo zimenezi. KB Mzimba KB, Nkhani yanu ndi yovuta kuimvetsa, komabe ndikuthandizani. Choyamba, kodi pamene mumagwirizana zomanga ukwati wanu, mudayamba mwakhala pansi nkukambirana za mapulani anu pa nkhani yokhala ndi ana kapena izi munagwirizana mutalowana kale? Ndikufunsa chifukwa ukwati ndi anthu awiri. Ine ndikuona ngati mwamuna wanu chilipo chimene sakufuna kuti mudziwe ndipo akunamizira kuti nonse mukulera. Zaka ziwiri mukutolera za mwana? Mukutolera chiyani? Mwanena kale kuti palibe chimene mukuona kuti mwatolerapo mpakana pano. Mumufunse ameneyo kuti nthawi yakwana tsopano kuti mulandire mphatso yomwe mwakhala mukuiyembekeza ija. Mumuuze kuti simupanganso zolera koma zenizeni, mumve chimene ayankhe. Ngati pali vuto lomwe akuchita nalo manyazi kukuuzani, mumuuze kuti asaope chifukwa inu ndi thupi limodzi-mavuto ake ndi anu omwe. Kuli asinganga odziwa kusula kunja kuno! Akakanika, kuchipatala amathandizanso! Ndani safuna mwana? Sakundilankhula Zikomo Anatchereza, Ndili pabanja ndi mkazi wina ndipo timakondana kwambiri. Koma akwawo sagwirizana nawo ndipo ngakhale akumane panjira salankhulana. Ngakhale ine ndikawalankhulitsa sandiyankha. Ndichitenji chifukwa ndikuopera mawa atadwala kapena kumwalira kumene. Thandizeni. ",12 " Nanawa: Mlowammalo wa kupitakufa Matenda a HIV/Edzi asokoneza miyambo ina monga mwambo wa kupitakufa, womwe umapereka mphamvu kwa fisi kuti akakonze maliro pocheza ndi namfedwa kwa sabata ziwiri ndipo machezawo amachitika katatu patsiku. Chifukwa cha matendawa, kwabwera njira ya nanawa yomwe yazilalitsa mwambo wa kupitakufawu. BOBBY KABANGO adali mboma la Nsanje komwe adacheza ndi mlembi wa nyakwawa Masanzo kwa T/A Mlolo. Chisale watuluka nkumangidwanso Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Kodi amfumu tawapeza? Ayi, iwowa adzukirira kudimba. Akuyembekezereka kubwerako madzulo chifukwa ntchito yakula kumeneko. Tidalire kuti inu mutithandiza pa vuto lathu? Musakaikenso, ndine mlembi wa amfumuwo ndiye palibe chomwe sindikuchidziwa chokhudza mudzi uno ndi miyambo yomwe timatsata. Mkaka: Mwambo wa nanawa timangomwa mankhwala othamangitsa imfa Kodi mwambo wa kupitakufa ukuchitikabe kuno? Zikuchitika koma mobisa chifukwa momwe matenda a Edzi aopseramu sungayerekeze kumachitabe mwambowu. Amabungwe akhala akufika kumemeza anthu kuti miyambo yoipa, monga umenewu, itheretu ndipo zipatso zake zikuonekadi pano. Ndiye mukutani kuti imfa ithawe pakhomo? Timagwiritsa mankhwala a nanawa amene amathamangitsa imfa pakhomo. Kuno anthu ambiri tikutsata zimenezi. Nanawa nchiyani? Ndi mankhwala amene singanga amachita pakhomo pamene pagwa maliro. Anthu, maka achibale, amamwa mankhwalawo molandirana ndipo pakhomopo pamakhala bwino. Zimachitika nthawi yanji? Maliro akachitika monga lero, mawa timakaika ndiye timasweretsa tsiku limodzi pamene timasonkhana kudzasesa. Nthawi yosesa mpamene mwambo wa nanawa umachitika. Mungathe kuchita mwambowu nthawi iliyonse kaya ndi masana kapena madzulo. Kodi mankhwalawa mumatemera kapena mumadya? Mankhwalawa ali pawiri. Ena amakhala a madzi. Amawaika mkapu ndiye aliyense wachibale amalandirana mankhwalawo kumamwa pangono mpaka nonse achibale akukwaneni. Pamene mankhwala ena amawaika kudenga kwa nyumba yomwe mumagona malemuwo. Mumawasomeka kudenga mbali yomwe kuli khomo kuti anthu akamalowa mnyumbamo azigwira mankhwalawo. Mukutanthauza wachibale aliyense amayenera amwe mankhwalawo? Zimatero kumene. Nonse mumalandirana, kumwa pangono basi, aliyense kamodzi komanso momapatsirana. Nanga achibale amene sadafike pamwambowo mumawatani? Achibale amene nthawi ya malirowo kapena tsiku la kusesalo palibepo, timawasungira mankhwalawo. Mankhwala ake ndi amene tawasomeka kudenga aja. Tsiku lomwe akonza zodzafika pakhomopo, timawalandira ndi kuwatengera kunyumba yomwe kudachitika malirowo. Ndiye pamene tikulowa mnyumbayo, timawapatsa mankhwala aja kuti agwire. Akangotero basi amabwezeretsa mankhwalawo kudengako. Amachitanso china chiti? Palibe, ngati agwira mankhwalawo ndiye kuti nawonso akonzedwa ku imfa yomwe idakangogwa pakhomopo. Nthawi yomwe munkatsata mwambo wa kupitakufa zinkakhala bwanji? Maliro akachitika chonchi, timapeza fisi kuti apite kunyumba yomwe kwachitika malirowo akacheze ndi namfedwayo. Katatu patsiku kapena zikavuta atha kumacheza nawo kawiri patsiku kwa sabata ziwiri. Fisiyu ntchito yake idali yoti achotse mzimu wa imfa womwe wakuta pakhomopo. Mpaka katatu? Ndiye zidalikolikotu Hahaha! Eeh, amasangalala kwambiri koma pano zimenezi zidatha. Nanga akamwalira wamkazi, afisi aakazinso amapezeka? Ayi, zikatere ndiye tinkapanga mankhwalawa kapena apo ayi mupemphe banja lina kuti likupitireni kufako. ",6 " Kusamala anapiye a mikolongwe Amati nkhuku ndi dzira, kusonyeza kuti ngati susamala dzira ndiye kuti udzalandira nkhuku za matenda zomwe sizichedwa kufa. Komanso kupanda kusamalira bwino anapiye, akhonzanso kufa. Koma chisamaliro ichi nchotani? BOBBY KABANGO adakacheza ndi Rose Mphepo, mphunzitsi wa kusukulu ya ziweto ya Mikolongwe mboma la Chiradzulu. Adacheza motere: Tidziwane mayi Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndine Rose Mphepo. Ndine Assistant Hatchery Managerwachiwiri kwa woyanganira malo oswera nkhuku. Koma tikuopeni? Mphepo kuyanganira anapiye Tikufuna timve momwe tingasamalire anapiye a mikolongwe. Kuno tilibe nkhuku mtundu wake mikolongwe. Anthu amangoti nkhuku za mikolongwe, koma palibe mtundu wa mikolongwe. Nkhuku zimenezi ndi ma Black Austrolorp koma chifukwa zimachokera kuno, anthu amangoti mikolongwe. Ndikufotokozerani momwe timasamalira anapiye koma tipite kuofesi kwathuko. Tsono tidaika madzi amene mukaponde musadalowe kuofesiko, madzi amenewo ndi a mankhwala kuti musabweretse matenda kukholako. Chisamaliro cha anapiye amtundu umenewu chimakhala chotani? Ngati ukufuna kuweta nkhuku zimenezi, choyamba samala mazira. Ndiye tili ndi khola ilo lomwe tikusungako nkhuku 300. Tambala mmodzi ali ndi misoti 10. Zimaikira komweko ndipo mmawa cha mma 10 koloko timakatolera mazira komanso madzulo cha mma 3 koloko. Mazira amenewa amapita kuti? Tikatolera, timapita nawo ku hatchery. Iyi ndi nyumba yofungatilitsa mazira kuti anapiye atuluke. Koma tisadawaike mnyumbayi, timawaika mu Egg Chamber. Awa ndi malo amene timasankhira mazira. Timaikapo zongendawa amene amapha timajeremusi tomwe dzira latenga kuchokera kukhola kuja. Timawasungamo kwa sabata imodzi. Tikawatulutsa mmenemu ndiye timawaika moti akafungatilitsidwe. Dzira ndi chinthu cha moyo, ngati taliyika mu incubator lili ndi majelemusi, ndiye kuti anapiye adzabadwanso ndi matenda. Komanso panthawiyo timasankha mazira amene ali ndi mavuto monga amene ali angonoangono komanso osweka. Fotokozani zomwe zimachitika mu incubator-mo. Incubator yathu imalowa mazira 30 000 koma chifukwa cha mavuto ena, sitikwanitsa kuikamo mazira 30 000, mapeto ake timangoika momwe tapezera koma sabata iliyonse Lachiwiri timatulutsa anapiye 4 000. Mavuto enanso nkuti tilibe zakudya zokwanira zosamalira anapiye ngati achuluka. Tikawaika mmenemu, timadikira padutse masiku 18, apa timasankha mazira amene satulutsa anapiye. Dziwani kuti tambala akaphonya pamene akukwera thadzi, dzira limenelo limakhala lakufa loti simutuluka napiye. Zimakhala bwanji kuti Lachinayi lililonse muzitulutsa anapiye? Nchifukwa choti sitiika mazira 30 000 monga ilili incubator-yi. Ndiye sabata ino timaikamo mazira, ena timaika sabata yotsatira, zomwe zimachititsa kuti anapiye azitulukanso mosiyana. Ena amatha masiku 21 sabata ino pamene ena sabata ya mawa. Kodi anapiye sangapse mmenemu atati atuluka chifukwa cha kutentha? Kutentha kwa incubator ndi kofanana ndi nkhuku, timaonetsetsa kuti incubator ikutentha madigiri 37.5. Magetsi akazima zimakhala bwanji? Magetsi akazima mutha kulumikiza jeneleta koma ngati mulibe ndiye azime kwa masiku awiri mutafungatilitsa mazira amene adutsa masiku 18, ndiye mazira onse amaonongeka. Amenewo katayeni chifukwa anapiye amakhala afa. Anapiye akabadwa, mumalowera nawo kuti? Amabwera mnyumba iyi. Ndi motentha chifukwa amakhala mwana wathu ali mchikuta. Kupanda kutentha kumeneku samachedwa kufa chifukwa ndi osakhwima. Katemera mumawapatsa atakula bwanji? Tsiku lomwe abadwa timapereka katemera woteteza ku matenda. Kenaka timawapatsa madzi ndiye timadikira padutse mphindi 30 tisadawapatse zakudya. Zikatha sabata imodzi, timazipatsa katemera wa gumbolo, sabata yachiwiri timazipatsa katemera wa LaSota, sabata yachitatu timawapatsa gumbolo, yachinayi LaSota, ndipo yachisanu wa firepox. Sabata ya 6 timawagulitsa kwa alimi ndipo mlimi savutika nazo. Alimi amagula K500 mwanapiye mmodzi. Nanga zakudya? Zakudya timapanga tokha, zikangobadwa kumene mpaka atakula timawapatsa chicken mash. ",4 "Apempha Akatolika Amvere Maepiskopi Awo pa Kapewedwe ka Coronavirus Akhristu a mpingo wa katolika mdziko muno awapempha kuti atsatire ndondomeko zomwe maepiskopi awo ananena kudzera muchikalata chomwe analemba sabata zapitazo, ngati njira imodzi yopewera mliri wa COVID-19. Analemba chikalata choyimitsa mapemphero mmatchalitchi onse Mkulu wofalitsa nkhani mu dayosizi ya Dedza, bambo Josephy Billiati ati chikalatachi chinapempha akhristuwa kuti asamakumane ku tchalitchi koma mmalo mwake azipemphera mnyumba zawo ndi cholinga chofuna kupewa kutenga kapena kufalitsa kachilomboka kudzera mu kukumana mmatchalitchi. Iwo atinso akhristuwa akuyenera kukhala omvera atsogoleri awo kuphatikiza pa ndondomeko zomwe dayosizi yawo yakonza. Zoonadi ma episkopi athu anatilembera kalata kuti tisamakumane kuti tipewe kufalitsa matenda a COVID-19 koma akhristu ena sakutsatira zimenezi. Koma ndi koyenera kuti tiphunzire kutsatira zomwe akuluakulu athu akutilamula, anatero bambo Biliati. Iwo pempha akhritsu kuti atsatire zomwe ma episkopiwa anapempha ndipo asadikire kuti mbindikiro uchite kuyamba. ",6 " Womukaikira zopakula ku Kapitolo adzipereka Adakali ku South Africa: Mphwiyo Wabizinesi Osward Lutepo, amene wakhala akusakidwa ndi apolisi a dziko lino, komanso polisi ya maiko osiyanasiyana ya Interpol, Lachitatu adatera mdziko muno kuchokera kunja ndipo adakadzipereka kulikulu la polisi ku Area 30 mumzinda wa Lilongwe. Lutepo, yemwenso ndi mmodzi mwa akuluakulu a chipani cholamula cha Peoples Party (PP), akumuganizira kuti amagwirizana ndi ogwira ntchito mboma ena kuti azipakula ndalama zaboma kupyolera mmakampani ake amene amalandira mamiliyoni ochuluka koma osagwira ntchito iliyonse. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Padakalipano, anthu oposa 20 akhala akukaonekera kukhoti pokhudzidwa ndi kusowa kwa mabiliyoni a boma. Ena mwa iwo amagwidwa ndi mamiliyoni osaneneka kumabuti a galimoto ngakhalenso mnyumba zawo, ndalama zimene akuganiza kuti zimasololedwa kunjira yolipirira pantchito ndi katundu yemwe boma limagula ya Integrated Financial Management System (Ifmis). Chongofika mdziko muno, Lutepo adapita kupolisi motsagana ndi womuimira pamlanduwo, Jai Banda. Wachiwiri kwa mneneri wa likulu lapolisi Kelvin Maigwa adati Lutepo, yemwe ndi wa zaka 35, adakadzipereka yekha. Tili naye ndipo tikumufunsa mafunso angapo. Padakalipano, milandu imene timuzenge sinadziwike, adatero Maigwa. Bungwe lothana ndi ziphuphu la Anti-Corruption Bureau (ACB) lidatseka mabuku akubanki a makampani 20 amene akuwakaikira kuti akukhudzidwa ndi chipwirikiti chopakula mabiliyoni a boma. Makampani 8 adali a Lutepo, kapena amene amayendetsa mogwirizana ndi anthu ena. Izi zili choncho, Pika Manondo, mkulu wina amenenso akusakidwa ndi apolisi pomuganizira kuti akukhudzidwa ndi mlandu wofuna kupha mkulu woonetsetsa kuti ndondomeko ya chuma cha boma ikuyendetsedwa bwino, Paul Mphwiyo, adauza nyuzipepa ya The Nation kuti abwera mdziko muno pofika mawa. Iye adati ndi wokonzeka kuthandiza apolisi pazofufuza zawo zokhudza kuomberedwakwa Mphwiyo pa September 13, 2013 pomwe amati azilowa pachipata cha nyumba yake ku Area 23. Nthawiyo nkuti Mphwiyo atagwira ntchitoyo kwa miyezi iwiri. Apolisi adanjata MacDonald Kumwembe yemwe adakhalapo msirikali, komanso Robert Kalua powaganizira kuti ndiwo adaombera Mphwiyo. Apolisiwo adagwiranso Dauka Manondo, mngono wake wa Pika. Kupakula kwa ndalama kwakhudza kwambiri boma la mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda, yemwe sabata zapitazo adachotsa nduna zake zina, kuphatikizapo yemwe adali nduna ya zachuma Ken Lipenga ndi yemwe adali nduna ya za malamulo Ralph Kasambara. Ndipo apolisi sabata yatha adakachita chipikisheni kunyumba kwa Kasambara, kuyangana galimoto imene akuti idagwiritsidwa ntchito pokaombera Mphwiyo, yemwe akadali ku South Africa ngakhale adatuluka kuchipatala kumene amalandira thandizo. ",7 "Chipatala cha Vatican Chasiyanitsa Ana Omwe Anabadwa Ophatana Chipatala cha likulu la mpingo wa katolika pa dziko lonse chachita opareshoni atsikana awiri omwe anabadwa mophatikana. Malinga ndi malipoti a Vatican Radio, chipatala cha ana cha Bambino Gesu mu mzinda wa Rome mdziko la Italy, chakwanitsa kupanga opareshoni atsikana awiri omwe anabadwa mophatikana ndipo pano atsikanawa ali bwino. Mayi ndi ana ake pambuyo powalekanitsa Atsikanawa anali ku chipatala china mdziko la Central African Republic chomwe Papa Francisco adachiyendera mchaka cha 2015. Ervina ndi Prefina ndi atsikana omwe adabadwa zaka ziwiri zapitazo ndipo iwo adabadwa ophatikana matupi. Kwa chaka chathunthu madokotala akhala akuwapima atsikanawa maka kuti apeze njira ya bwino yoti nkuwathandizira kuti choncho aliyense athe kukhala payekha osadalira ziwalo za thupi la mzake. Poyamba anawo amawoneka chonchi Malipoti ati mkulu woyendetsa chipatala cha ana cha Bambino Gesu cha likulu la Mpingo wa Katolika pa dziko lonse, Vatican, chomwe chili ku Rome mdziko la Italy Mariella Enoc anali ku Bangui mdziko la Central African Republic komwe kulinso chipatala cha ana chomwe chimalandira thandizo kuchokera ku Vatican ndipo Papa Francisco adayendera chipatalachi pomwe anakacheza mdzikolo mchaka cha 2015. Atawaona anawa Enoc anaganiza zowatumiza anawa moperekezedwa ndi mayi a anawa ku Rome. Masiku apitawa madokotala anawapanga opareshoni yowasiyanitsa matupi yomwe malipoti akuti inayenda bwino. Ndipo naye mayi wa anawa wati anawa ali bwino moti akusewera ndi kuchita zonse zomwe ana amachita ndipo akuti nao anawa akufuna adzakhale madokotala kuti adzathandize anthu ena. Mmawu ake mayi wa anayu wati akuthokoza anthu osiyana-siyana omwe agwira ntchito yotamandikayi ndipo mwa njira ya padera Papa Francisco chifukwa cha chithandizo chomwe akupereka kwa ana osiyana-siyana. Opareshoni ya anawa akuti inali ya maola 18 ndipo madokotala ndi anamwino opitirira 30 ndi omwe anagwira ntchitoyi. Ervina ndi Prefina anabadwa pa 29 June mchaka cha 2018 pa tsiku lomwe Mpingo wa Katolika pa dziko lonse umachita chaka cha Petulo ndi Paulo Oyera. ",6 " Mtsutso pa za makanda odabwitsa Mtsutso wakula ngati nkoyenera kuti ana obadwa modabwitsa azituluka mchikuta. Izi zadza mwana wina wankhope yodabwitsa atabadwa kuchipatala cha Salima sabata yatha. Mwanayo adamwalira Loweruka pachipatala cha Lilongwe. Izi zidachitika patangotha sabata zochepa kuchokera pomwe mwana winanso yemwe adabadwa wopanda maso, mphuno ndi makutu adabwadwa ku Nkhotakota. Uyonso adatisiya. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Pomwe ena akuti ndi bwino kutsatira zomwe zinkachitika kale, kuti ana otere samatuluka mchikuta, ena akuti kutero nkulakwa chifukwa ndi kuwaphera ufulu wokhala moyo anawo. Mayi wina wa ku Chilomoni, mumzinda wa Blantyre, Martha Banda, akuti ngakhale akudziwa kuti kupha nkulakwa, si bwino kulola anawo atuluke mchikuta chifukwa adzazunzika. Mzamba wina wodziwa zitsamba ku Mchinji, Ethel Kwitanda, wati kale anaotere sankatuluka mchikuta koma pankachitika nkhanza moti mpaka mwina moyo wa munthu umatha kupita. Mwana akabadwa ndi ziwalo zodabwitsa akuluakulu ankatha kumupitiriritsa dala mchikuta momwemo moti nthawi zina mayi wake sankazindikira. Ena ankakhulupirira kuti mwanayo amabweretsa mavuto. Amatha kumupitiriritsa dala nkukanena kuti wabwera wakufa kale, akutero Kwitanda. Koma Dr Adamson Muula, mmodzi mwa adotolo a nthenda zofala, wati si bwino kuchotsa moyo wa mwana pongotengera momwe akuonekera, polingalira kuti moyo ndi chimodzimodzi, osalingalira za momwe khanda likuonekera. Funso loti tidzifunse ndi loti kodi kuoneka mosiyana ndi ena kungapangitse khanda kuti lisakhale munthu? Khanda lobadwa mwa mayi ndi bambo ndi munthu basi. Kodi tikapha ana obadwa mosiyana ndi ena, kenako tidzapha ndani? akudabwa Muula. Mmodzi mwa akadaulo oona za momwe anthu amaganizira Symon Chiziwa akuti nkhani ya ana obadwa modabwitsa yakhala ikuzunguza anthu ambiri padziko lapansi. Ana otere akabadwa kumakhala manongonongo. Nthawi zambiri azamba amangowasiya anawo kuti afe. Makolo amangouzidwa kuti anawo apitirira, akutero Chiziwa. Iye wati ena amakhulupirira kuti makolo akhoza kuvutika kwambiri kusamalira ana otere, komanso kuti akhoza kuwabweretsera matsoka. Kalekale ku Greece ana otere akabadwa amatsamwitsidwa kapena kumizidwa. Mwana akabadwa, makolo amayenera kupititsa anawo kwa akuluakulu ndipo akaona kuti kalibe ndi moyo wamphamvu, amakasiya poyera chifukwa amati sikadzakhala nzika yodalirika, iye akutero. Koma izi zili choncho, Chiziwa akuti anthu amadziwa kuti moyo ndi chinthu chamtengo wapatali choncho kukonza makanda chifukwa cha ichi nkulakwa. Makolo amakhulupirira kuti akabereka, alera ana kuti adzaime paokha. Ana otere zikhoza kukhala zovuta kuti adzaime paokha. Choncho nkhaniyi ndi yofunika kufunsa makolowo maganizo awo, akutero Chiziwa. Malamulo a dziko lino amapereka ufulu wokhala ndi moyo kwa munthualiyense. Gawo lachinayi la malamulo oyendetsera dziko lino limati: Munthu aliyense ali ndi ufulu wokhala ndi moyo ndipo palibe munthu yemwe ali ndi mphamvu zochotsa moyo wa mnzake pokhapokha imfayo yagamulidwa ndi khothi lodziwika bwino litamupeza munthu woti aphedweyo ndi mlandu wofunika kulandira chilango chotero potsatira zomwe malamulowo akunena. Mkulu wa Bungwe la anamwino ndi azamba mdziko muno Harriet Kapyepye wati mchitidwewu unali wozunza mizimu ya anthu osalakwa pogwiritsa ntchito mfundo zopanda pake. Iye adati aliyense ali ndi ufulu wokhala ndi moyo ngakhale atabadwa ndi vuto lalikulu chotani. Kapyepye wati anamwino ndi azamba amdziko muno amaphunzitsidwa mmene nkhanza zoterezi zingapeweredwe komanso amaphunzitsidwa mmene angalangizire amayi omwe amapempha okha kuti mwana yemwe wabadwa ndi chilema amuphe komanso kuti amulandire mbanjamo. Ife pantchito yathu timaonetsetsa kuti mwana aliyense yemwe wabadwa akhale ndi moyo komanso asanyozeke chifukwa cha chilema. Tili ndi mabungwe osiyanasiyana omwe timatha kutumizako ana amavuto ena ndipo amatha kukonza mavuto ngati amenewo, akutero Kapyepye. ",19 " A Malawi akufuna 2018 wa ngwiro Pomwe chaka cha 2018 changoyamba kumene, mtsogoleri wa zipani zotsutsa boma Lazarus Chakwera ndi akadaulo ena ati boma lisinthe kayendetsedwe ka zinthu kuti chakachi chikhale chokomera Amalawi. Chakwera yemwe ndi mtsogoleri wa chipani cha Malawi Congress Party (MCP), kadaulo pa zamaphunziro Benedicto Kondowe, kadaulo pa zachuma Dalitso Kubalasa, kadaulo pa zaumoyo George Jobe ndi mtsogoleri wa bungwe la alimi la Farmers Union of Malawi (FUM) Alfred Kapichira Banda aunikira momwe zinthu zikuyenera kuyendera. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Chakwera: Amalawi amayembekeza zambiri Akuluakuluwa akhala akudzudzula za momwe boma limayendetsera zinthu zina mchaka chomwe changothachi ndipo poomba mkota wa madandaulo, Chakwera adati boma lidalephera kukwaniritsa malonjezo ake. Padali zinthu zambiri zomwe Amalawi amayembekezera potsatira malonjezo omwe boma lidalonjeza koma momwe chaka cha 2017 chimapita kumapeto, padalibe chomwe chidaonekapo, adatero Chakwera. Iye adati mwa zina, boma lidalonjeza kusintha nkhani ya kuthimathima kwa magetsi zomwe sizidatheke mpaka pano, kutukula alimi koma mmalo mwake ndiwo adamva kuwawa kwambiri mchakachi, kuthana ndi katangale zomwe sizidatheke komanso kulemekeza malamulo. Akuluakuluwa amalankhula ndi Tamvani potsatira mawu a pulezidenti Peter Mutharika polandira chaka chatsopano pomwe adati Amalawi ayembekezere chaka chopambana cha zitukuko. Mu 2018, titsegulira ntchito yaikulu ya mthirira yomwe idzapindulire mabanja pafupifupi 40, 000, tipitiriza kutsegula mwayi wa ntchito kwa achinyamata, ntchito za mtukula pakhomo ndi ngongole za achinyamata ndi amayi, adatero Mutharika. Kudali kugona kuchigayo kudikira magetsi ayake Iye adatinso boma lipitiliza kutukula ntchito za chuma powonetsetsa kuti chiwongola dzanja chomwe anthu amapeleka akakongola ndalama ku mabanki chatsika kuti anthu ambiri azitha kutenga ngongole. Ndikufuna mchaka chimenechi, mlimi, mphunzitsi, namwino, msilikali ndi apolisi azitha kulowa mbanki nkutulakamo atatenga ngongole kuti adzipezere malo ndikumanga nyumba zawo, Mutharika adatero. Iye adati boma lake lili ndi ndondomeko zomwezidzathandize kuti vuto la magetsi lisadzawonekenso mdziko muno likangotha. Powonjezerapo pa malonjezowa, nduna ya zamalimidwe, mthilira ndi chitukuko cha madzi Joseph Mwanamvekha adati mchaka cha 2018 boma lipezera alimi misika yabwino ya zokolola kuti apukute misozi yawo. Chaka chatha sitikadachitira mwina koma kutseka zipata kuti mbeu zisatuluke mpaka tigule chakudya chokwanira koma poti chaka chino chakudya chiliko kale chokwanira, alimi ayembekezere misika yabwino, adatero Mwanamvekha Koma chakwera adati, Bola izi zisakhale zongofuna kupeleka chiyembekezo kwa Amalawi kuti aziti boma litithandiza. Nthawi yopanga ndale zonamiza anthu idatha, pano ndi nthawi yolankhula ndi ntchito. Pounikira za momwe chuma chikuyenera kuyendera, Dalitso Kubalasa yemwe ndi kadaulo pa za chuma adati boma likuyenera kumanga mabawuti kuti nthambi zonse za boma zizitsatira malamulo oyendetsera chuma cha boma. Iye adati mu 2017, nthambi zina za boma zidapezeka ndi mirandu yosapeleka malipoti a kayendetsedwe ka chuma cha boma zomwe ziapangitsa kuti papezeke mavuto ambiri pa kauniuni wa chuma ha bomachi. Tidaona mmene malipoti adalili mchakachi okhudza kauniuni wa chuma cha boma pomwe ndalama za nkhaninkhani sizidaoneke momwe zidagwirira ntchito. Pamenepa pakuyenera kusinthidwa mchakachi, adatero Kubalasa. Iye adati ngati izi sizitheka, ndiye kuti Amalawi ayembekezere chaka china chowawa ku mbali ya za chuma ndipo mabala ake adzavuta kupola kaamba koti chaka chotsatiracho ndi chachisankho. Benedicto Kondowe yemwe ndi mkulu wa mgwirizano wa bungwe oyanganira za maphunziro adati boma lisakakamire kutsegula sukulu zokha ndi kusintha maphunziro koma kuti liyike mtima kwambiri pa maphunzirowo apamwamba. Iye adati maphunziro otukula aphunzitsi apite patsogolo, sukulu zikhale ndi aphunzitsi okwanira, zipangizo zophunzilira ndi ndi kuphunzitsizira zizipezeka mokwanira ndipo oyendera sukulu akhale odzipeleka. Ndibwino kuti sukulu zikutsegulidwa koma tikuyenera kuwonetsetsa kuti zipangizo zilimo, aphunzitsi ndiwokwanira komanso ophunzitsidwa bwino ndipo pakhale timu ya akadaulo oyendera kuwona kuti maphunzirowo akuyenda bwinodi, adatero Kondowe. Kadaulo wa zaumoyo George Jobe wati potukula ntchito za umoyo, boma liyambe kukwaniritsa mlingo wa mgwirizano wa mayiko oyika K15 pa K100 mu bajeti yake yopita ku unduna wa zaumoyo. Iye wati mpofunikanso kukhwimitsa malamulo olangira anthu opezeka akuzembetsa mankhwala ndi zipangizo za chipatala kuti zipangizo zoterezi zizikhalamo mzipatala nthawi zonse. Nkhani yayikulu apa ndi kukhulupilika ndi kukhala ndi ndondomeko zokhwima bwino zotetezera zipangizo za chipatala. Pamenepa pakukhudzidwanso ndi kukhala ndi ogwira ntchito za chipatala okwaira, adatero Jobe. Pulezidenti wa alimi Alfred Kapichira Banda adati alimi sakufuna zambiri koma kudzipeleka ku mbali ya boma pa nkhani yotukula alimi makamaka pa nkhani yolimbana nsi mbozi zomwezikuvuta komansomisika. ",11 "Akhristu Apewe Kuyika Mtima pa za Mdziko-Papa Mtsogoleri wa Mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisko wati akhristu aleke kuyika mtima kwambiri pa zinthu za mdziko la pansi. Papa Francisko walankhula izi lachiwiri pa nsembe ya misa yomwe anatsogolera ku likulu la mpingowu ku Vatican. Iye wati kuika mtima kwambiri pa zinthu za dziko lapansi kumachititsa anthu kukhala mu mdima wosasiyanitsa pakati pa chinthu chabwino ndi choipa. Papa Francisko Pamenepa Papa Francisko wapempha anthu kuti akhazikike nthawi zonse pa zinthu zomwe ndi zokweza ufumu wa Mulungu. Polankhula mtchalichi cha lalingono la Santa Marta ku Vatican, Papa Francisko wati mavuto ambiri monga katangale ndi ziphuphu akhazikika pakati pa anthu chifukwa choika mtima kwambiri pa zinthu za dziko lapansi mmalo motsogoza Mulungu. Papa Francisko wati anthu akuyenera kumadzifunsa nthawi zonse ngati chomwe akufuna kuchita chikuchokera kwa Mulungu kapena mzimu woipa. Pamenepa iye wati munthu aliyense akuyenera kumasinkhasinkha nthawi zonse zomwe zikuchitika pa moyo wake kuti adziwe ngati akuchita zosangalatsa Mulungu kapena ayi. Pomaliza iye wati nkofunika kumapemphera kwambiri pofuna kuima njiiii pa za Mulungu. ",13 " Msika wa osewera watentha Pamene matimu ali kopumira kukonzekera ndime yachiwiri ya 2015 TNM Super League, msika wa osewera wafika potentha pamene matimu ali kalikiriki kugula ndi kugulitsa osewera ncholinga chofuna kuchita bwino mligiyi ikayamba mndime yachiwiri. Tiyamba ndi timu yomwe ikuteteza ligiyi yomwenso ikutsogola ndi mapointi 32. Iyi ndi Big Bullets, yomwe padakalipano ikukambirana ndi timu ya Mzuni FC kuti itenge mnyamata womwetsa zigoli wa ku Burundi, Aimable Niyikiza, amene tikukamba pano ali kukampu ya Bullets. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Timuyi ikufunanso itenge mnyamata wosewera pakati kutimu ya Azam, Yamikani Chester, koma timu yakeyi ikukaniza kuti wosewerayu sali pamalonda. Bullets yatenganso Chisomo Mpachika wosewera kumbuyo mtimu ya Dedza Young Soccer ngakhale timu yake ikukaniza kumugulitsa ponena kuti ngati Bullets ikumufuna ndiye iwapatse Sankhani Mkandawire ndi Yamikani Fodya. Tipite ku Silver Strikers yomwe yakanika kutenga goloboyi wa Mighty Be Forward Wanderers Richard Chipuwa ndipo mmalo mwake yatenga Bester Phiri, yemwenso amagwirira pagolo ku Wanderers. Padakalipano Wanderers yatchaja Silver kuti ipereke K2 miliyoni pokana kuti Silver itenge wosewerayu pangongole. Silver yatenga kale John Banda yemwe adali pangongole ku Young Soccer kuchokera ku Evirom pamtengo wa K500 000. Timuyi ikufunanso kutenga mnyamata wosewera kumanzere chakumbuyo kwa Epac, Dalitso Mwase, pamtengo wa K2 miliyoni. Nayo Wanderers ikufuna kutenga Boston Kabango kuchokera ku Epac pamtengo wa K3 miliyoni. Koma Silver ndi Fisd Wizards nawonso maso awo ali pa mnyamata yemweyu. Wanderers ndi Bullets akulimbirananso Chester, yemwe Azam ikukanitsitsa kugulitsa. Wanderers yaonetsanso chidwi kufuna kutenga Kelvin Hara, Dave Mwalughali, George Hawadi ndi Hastings Banda komanso George Kasambara kuchokera kutimu ya Chilumba Barracks ngakhale timuyi ikukana kuti sakuwagulitsa osewera awo. Timuyi ikufunanso itenge John Lanjesi wa Civo pamtengo wa K4.5 miliyoni. Azam Tigers yatenga kale Abraham Kamwendo kuchokera ku Blantyre United ndipo yatoleranso osewera ena achisodzera pamene Moyale yatenga Komani Msiska yemwe akutsogola ndi zigoli ku Chilumba. Red Lions yagula wosewera wapakati wa Zomba United Stanley Dube. Mphunzitsi wa timuyi Collins Nkuna akuti wakhala akuyendayenda mmidzimu ndipo wapeza osewera ambiri mboma la Salima. Civo United sikumveka kuti ikusaka osewera mitunda iti koma timuyi yaitanitsa Josophat Kwalira kuchokera ku Dedza Young Soccer. Wizards yatola Godfrey Masonda. Fisd ikufunanso kugula Precious Msosa kuchokera ku Wanderers. Msikawu utsekedwa pa 18 September usiku ligiyi isanayambirenso pa 19 September. ",16 "YODEP Ipereka Mbuzi kwa Ana Olumala Wolemba: Thokozani Chapola Bungwe la Youth and Development Productivity (YODEP) lapereka thandizo la chimanga komanso mbuzi kwa ana omwe ali ndi ma ulumali osiyanasiyana mboma la Zomba. Mkulu woona za mapulogalamu ku bungweli a Joy Mwandama, ati bungwe lawo lachita izi ngati njira imodzi yofuna kuwalimbikitsa anawa kupeza chakudya pomwe akumapita ku sukulu. Pamenepa a Mwandama alangiza makolo a anawa, kuti asamachite manyazi pomwe akufuna kutumiza anawa ku sukulu, ponena kuti aliyese ali ndi ufulu wolandira maphunziro mdziko muno. Makolo ena amachita manyazi ndi ana awo chifukwa ndi olumala koma sizimayenera kukhala choncho ayi mwana aliyense atumizidwe ku sukulu posatengera kuti ndi olumala kapena wa lungalunga, anatero a Mwandama. Mwa zina bungweli laperekanso ndalama zokwana 3 hundred sauzande kwacha kwa anawa. Mai Nduuzayani Wasili a mmudzi mwa Makambanjira ndi mmodzi mwa makolo a anawa ndipo ayamikira bungweli kaamba ka thandizoli. Zomwe achita a bungwezi ndi zosangalatsa chifukwa zipangitsa kuti miyoyo ya anawa pamodzi ndi ife ipite patsogolo, anatero mayi Wasili. ",14 " Shuga apezeka posachedwaIllovo Mkulu wa kampani yopanga shuga ya Illovo Malawi Mark Bainbridge wati kampaniyo iyesetsa kuti shuga azipezeka chaka chonse osati kumasowa momwe zakhalira sabata zingapo zapitazi. Bainbridge adanena izi Lachitatu pomwe nduna ya zokopa alendo ndi malonda Joseph Mwanamvekha adayendera kampaniyo kuti akamvetsetse za gwero la kusowa kwa shugayo. Kusowa kwa shuga kudachititsa kuti ogulitsa akweze kuchoka pa K750 kufika pakati pa K950 ndi K1 200. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Ogwira ntchito ku Illovo pakalikiliki kupanga shuga Malinga ndi Bainbridge, chaka chino kampaniyo inagulitsa shuga olemera matani 244 000, pomwe dziko lino limalira matani 160 000 ndipo anadabwa kuti shugayo akusowa bwanji. Tinali ndi shuga wokwanira chaka chino ngakhale mvula siyinagwe bwino nthawi yomwe timabzala nzimbe. Ogulitsa ena amagula shuga wochuluka nkumusunga zomwe zimadzetsa mavuto ngati awa, adatero iye. Iye adati padakalipano, kampaniyo ikuyesetsa kuti iwonjezere shuga amene imapanga kuti azikwanira chaka chonse. Mwanamvekha adati ndi wokondwa chifukwa kampaniyo yalonjeza kuti izipanga matani 650 a shuga patsiku, pomwe dziko lino limalira matani 411 patsiku. Tazindikira kuti pali shuga wochepa pamsika, zimene zachititsa kuti mtengo ukwere. Kwa amene akukweza shuga mopweteka Amalawi, malamulo agwirapo ntchito. Tili ndi chiyembekezo kuti Illovo ikwaniritsa lonjezo lake kuti shuga ayambe kupezeka, adatero Mwanamvekha. Pomwe Amalawi akudikira shugayo kuti ayambe kupezeka, Amalawi amene tidacheza nawo anadandaula ndi kusowa kwa shugako, ponena kuti izi zikuchititsa moyo kuthina. Mmodzi mwa Amalawiwo, Joana Chimphamba wa kwa Senti ku Lilongwe, adati abizinesi ena kumeneko akumaphwatula paketi ya kilogalamu imodzi ndi kuigawa pawiri. Gawo lililonse akuligulitsa K600 kapena K650. Izi zikutanthauza kuti yomwe timagula K780 pa paketi tikugula K1 200 kapena K1 250. Nanga akapitirira kusowa shugayu, zitithera bwanji? adadabwa iye. Chimvano Moyo wa ku Area 25 wati poyamba sadakhulupilire atatuma mwana kukagula shuga Lamulungu lapitali ndipo pobwera adamuuza kuti adagula pa mtengo wa K970 chikhalirecho, amagula pamtengo wa K780. Iye wati atapita kukatsimikiza kumsika, adapeza kuti magolosale ambiri alibe shuga ndipo pomwe adamupezapo adamutsimikizira kuti shuga akusowa ndipo akapezeka akukhala okwera mtengo. Mmodzi mwa anyamata ogwira ntchito mushopu yaikulu ya Spar mumzinda wa Lilongwe adati patenga nthawi shopuyi isanalandire shuga kuchokera ku Illovo. Iye adati anthu ambiri akhala akubwerera mushopuyi akafuna shugayo ngakhale kuti eni ake adapereka kale oda ya katunduyu koma sadanene kuti shugayo samabwera chifukwa chiyani. Ndipo mumzinda wa Blantyre, anthu ochuluka amakhamukira kusitolo zosiyanasiyana monga Shoprite kumene kumakhala miyandamiyanda ya anthu pamzere kufuna kugula shuga akapezeka. Davie Chilikumwendo wa ku Namiyango mu mzinda wa Blantyre adati wasiya kumwa tiyi chifukwa ndalama ya shuga siyikukwanira. Shuga yemwe akupezeka akugulitsidwa pamtengo wokwera. Padakalipano tizigwiritsa mchere mphala ndipo tiyi adzamwedwa shuga akayamba kugulitsidwa pa mtengo woyenera, adatero Chilikumwendo. Nawo ochita malonda mumzindawu ati kusowa kwa shuga kukusokoneza bizinezi chifukwa amadalira yemweyi popanga phindu lochuluka. Mmodzi mwa iwo, Clement Chafoteza wa ku Chilobwe, adati shuga wochepa yemwe akupezeka akugulidwa modula ndipo anthu wamba akukanika kuagula. ",2 "Dayosizi ya Mangochi Yapereka Ndondomeko Zatsopano Zopewera COVID-19 Mpingo wa katolika mu dayosizi ya Mangochi walangiza akhristu ake ndi njira zatsopano zomwe akuyenera kutsatira pochita mapemphero, potsatira kupitilira kufala kwa mliri wa Coronavirus mdziko muno. Walemba kalatayo-Bishop Stima Kalata yomwe yalembedwa ndipo yasayinidwa ndi episkopi wa dayosiziyi ambuye Montfort Stima, yapempha akhritsu kutsatira njira zina zowonjezera pamene akupitilira kutsatira njira zomwe mpingo komanso boma linakhazikitsa kale. Zina mwa njira zatsopanozi ndi monga kuvala chotchingira kukamwa ndi mphuno pamene akuchita mwambo wa nsembe za misa. Zina ndi monganso kukhala malo odutsa mpweya pamene akuchita mwambo wa mapemphero komanso kupewa kugwiritsa ntchito ma fan; kugwiritsa ntchito sopo komanso kulolini pamene akukonza mmalo opempherera, kukhala motarikirana ma mita awiri komanso kusamba mmanja ndi sopo. Ambuye stima kudzera mu kalatayi yomwe alembera ansembe, asiteri komanso akhristu eni ake, ati miyambo ya nsembe ya misa idzichitika kosapitirira ola limodzi ndipo akhristu apewe kupereka mphatso pamanja, kulandilira ukalistiya mmanja komanso ati pakuyenera kukhala ndondomeko yabwino komanso yokhazikika pamene akhritsu akutuluka mu tchalitchi kuti apewe kugundana-gundana. Pomaliza kalatayi yaimitsa ena mwa masakramenti monga sakrameneti la ubatizo, zinamwali za mpingo komanso maphunziro akatikisimu wa ana. Ngakhale izi zili chomwechi, episkopiyu wapereka chilorezo kwa masakramenti ena koma motsatira ndondomeko zopewera mliriwu. Ma sacramentiwa ndi monga la kulapa, kudzodza komanso ukwati pomwe akuti opereka komanso olandira ma sacramentiwa onse adzivala chotchingira kukamwa ndi mphuno komanso azitsatira ndondomeko zonse zomwe mpingo komanso boma lakhazikitsa. Pomaliza ambuye stima apempha akhristu kuti akonde kutsatira njira zozitetezerazi kulikonse ngakhale kumalo oti si kutchalitchi. ",6 "Maepiskopi ati ndi Okonzeka Kuthandiza Anthu Odwala Matenda a COVID-19 Maepiskopi a mpingo wa katolika mmaiko a Malawi, Zambia komanso Zimbabwe ati ali limodzi ndi anthu onse omwe akukhudzidwa ndi mliri wa CoronaVirus omwe wavuta kwambiri padziko lonse kuphatikizapo mmaiko atatuwa. Mu uthenga wawo wa Pasaka wopita kwa atumiki onse, akhritsu komanso anthu akufuna kwabwino, ma episkopiwa ati mliriwu, wasokoneza kwambiri chikondwelero cha Pasaka cha chaka chino, choncho pofuna kuonetsa umodzi wawo ndi akhristu onse komanso anthu omwe pakadali pano akudwala nthendayi,iwo akuwayikiza mmapemphero anthuwa kuti Mulungu awachiritse. Mu kalata yomwe yalembedwayi ati, ena mwa anthu, akukhala mwa mantha kamba ka mliriwu, komanso kuti achibale awo ena, akusungidwa ku malo awokha, zomwe zikukulitsa kutaya mtima pakati pawo, choncho iwo ati uthenga wa Pasakawu, uwalimbikitse za chikondi cha Mulungu. Onse omwe akudwala matendawa ndi omwe akuthandiza odwalawa akuyenera kudalira Mulungu, komanso polimbana ndi matendawa akhristu akuyenera kutsatira zomwe Papa Francisco anapempha kuti kusonkhedwe limodzi limodzi kuti tithadizire onse omwe akhuzidwa, yatero kalatayo. Iwo apemphaso akhritsu kuti akhale olimba mtima monga momwe akazi awiri aja analili pokawona manda a Ambuye Yesu, zomwe zikusonyeza kuti zonse zatha ndipo nayo imfa yagonja. ",6 "Anthu a Ulumali Sanachite Bwino pa Chisankho-MUB Bungwe lomenyera maufulu a wanthu osaona mdziko muno la Malawi Union of the Blind (MUB) lati anthu ambiri osaona omwe anapikitsana nawo pa chisankho chapitachi sanachite bwino kamba koti anthu ambiri mdziko muno adakalibe maganizo oti anthu osaona sangathe kuwathandiza pa ntchito zotukula dziko lino. Mkulu wa wabungwe-li mdziko muno a Ezekiel Kumwenda amayankhula izi kwa mtolankhani wathu amene amafuna kudziwa nambala ya anthu osaona omwe anapambana pa mipando yosiyanasiyana yomwe amapikitsana nawo pa chisankhochi. Kumwenda: Anthu ambiri sanawakhulupilire anthu osawona A Kumwenda ati ndi zomvetsa chisoni kuti mwa anthu asanu ndi mmodzi (6) omwe amapikisana nawo pachisankhochi mmodzi yekha ndi amene wapambana pa mpando wa ukhansala mdera lina mboma la Machinga. Anthu ambiri sanawakhulupilire anthu osaona kuti angawatsogolere pa mipando yosiyanasiyana, anatero a Kumwenda. Iwo anaonjezera kuti vuto la kusowa kwa ndalama zochititsira misonkhano yokopa anthu ndi lomwe lawonjezeranso kuti anthu wa asachite bwino pa zisankhozi. A Kumwenda ati ali ndi chiyembekezo kuti chiwerengero cha anthu osaona omwe adzapikisane nawo pa chisankhochi mchaka cha 2024 chidzakhala chokwera kamba koti chimenechi chinali chiyambi chabe. ",11 " Makhoti ayambanso kugwira ntchito Sitalaka yomwe ogwira ntchito mmakhoti amachita yatha Lachinayi. Mtsogoleri wa ogwira ntchitowa, Charles Lizigeni, adatsimikizira Tamvani kuti makhoti onse a mdziko muno ayambanso kugwira ntchito. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Tagwirizana zobwerera kuntchito kaamba koti Amalawi amavutika kuti apeze chilungamo chifukwa cha sitalakayi, adatero Lizigeni. Ogwira ntchito mmakhoti atenga masabata anayi akunyanyaka ntchito pofuna kukakamiza boma kuti liziwapatsa ndalama zolipirira nyumba ngati momwe likuchitira ndi majaji ndi mamajisitiliti. Koma nduna ya zachuma, Goodall Gondwe, idali yodabwa kuti majaji ndi mamajisitiliti akulandirira padera ndalama zolipirira nyumba. Boma lidasintha ndondomeko zolipirira ogwira ntchito ake mu 2014 moti munthu aliyense sakuyenera kulandirira padera ndalama za nyumba. Malipiro omwe ogwira ntchito ntchito mboma amalandira [clean wage] adaphatikizamo kale malipiro apamwezi a munthu ndi ndalama zolipirira nyumba. Ngati majaji ndi mamajisitiliti akulandirira padera ndalama za nyumba ndiye kuti boma lidangolakwitsa, idatero ndunayo. Boma, kudzera mwa mlembi wa zachuma Ben Botolo, lidadzudzula ogwira ntchitowa ndipo lidawauza kuti sitalaka yawo siyovomerezeka ndi malamulo a dziko lino. Boma lidauza anthuwo kuti abwerere ku ntchito. Botolo adati nzosatheka kuti boma liziwapatsa ndalama za nyumba zoyambira mchaka cha 2012. Koma Lizigeni adatsutsa zomwe mlembiyu adalankhula. Sitalaka yathu ndi yovomerezeka. Ngakhale tikubwerera kuntchito sizikutanthauza kuti sitalaka yathu idali yosavomerezeka. Anthuwa adayenera kuyamba ntchito Lachitatu, koma adakana kutero ndipo adapempha kuti apolisi omwe adadzadza mmakhoti achokeko kaye. Sitalakayi idayamba pa July 31 mmakhoti onse a mdziko lino. ",11 "Mayi Akagwira Ukayidi kwa Zaka Zitatu Kamba Kovulaza Ana Owapeza Bwalo la milandu ku Lilongwe lalamula mzika ina ya ku Rwanda Silvia Mukunoheri wa zaka 25 kuti akakhale ku ndende ndi kugwira ntchito ya kalavula gaga kwa zaka zitatu kamba kovulaza ana owapeza. Miyendo ya ana amene anavulazidwawo Malinga ndi woyimira boma pa milandu Sergeant Abigail Chirwa, pa 3 March chaka chino mayiyu adapezeka akukakamiza ana awiri omwe ndi owapeza kuti akwawe pansi pokhakhala dzuwa likuswa mtengo ati kamba kowononga shuga komanso mpunga. Atawonekera ku bwalo la milandu, Mukunoheri anawukana mlanduwu zomwe zinachititsa woyimira boma pa mulandu kuti abweretse mboni zinayi zomwe zinachititsa kuti mayiyu apezeka olakwa. Popereka chigamulo chake Magistrate Sarah Beza anati zomwe anachita mayiyu ndi zosemphana ndi gawo 254 la malamulo a dziko lino ndipo anamulamula kuti akakhale ku ndende ndi kukagwira ntchito ya kalavula gaga kwa zaka zitatu. ",7 " Bzalani mbewu zocha msangaLipita Woyendetsa ntchito za ulangizi ndi njira zamakono za ulimi muunduna wa zamalimidwe, Wilfred Lipita, wati alimi akuyenera kutengerapo phunziro pa zomwe zidaoneka muulimi wa chaka chatha ndi kusankha mwanzeru mbewu zolima chaka chino. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Polankhula ndi Uchikumbe paulangizi, Lipita adati masiku ano nkovuta kutchera kuti mvula iyamba lero ndipo idzatha mawa mmalo mwake njira yabwino nkusankha mbewu zocha msanga. Upangiri wa zanyengo ndi umenewo komanso payekha mlimi ayenera kukhala wozindikira kumwamba kukhoza kusintha nthawi iliyonse malingana nkusintha kwa nyengoku, adatero Lipita. Lipita: Alimi ena apulumukira chinangwa Iye adati kunjaku kuli mbewu zocha msanga zomwe mvula itati yadulira panjira, mlimi akhoza kupeza popumira kusiyana nkukakamira mbewu zokhalitsa mmunda chifukwa izi ndizo zingalowetse njala. Mkuluyu adatinso pomwe alimi akubzala mbewu zachizolowezi monga chimanga, nyemba, fodya ndi zina ayeneranso kulingalira za mbewu zina zopirira kuchilala monga chinangwa ndi mbatata. Mu ulangizi wake, Lipita adati alimi ena chaka chino apulumukira chinangwa ndi mbatata kupatula ulimi wa mthirira malingana nkuti ulimi chaka chatha sudayende bwino chifukwa cha mvula yokokolola ndi ngamba. Mbewu ngati chinangwa zili mgulu la mbewu zomwe timati zachitetezo chifukwa ngakhale mvula idule, izo zimaberekabe. Palibe kanthu kuti mitsitsi yake ndi yaikulu kapena yochepa bwanji koma nkhani ndi yakuti mbewu zina zitakanika, mlimi amakhala ndi pogwira, adatero Lipita. Mmadera ambiri chimanga chidatuluka ndipo mlangizi wamkuluyu adati imeneyi si nkhani yokhazikika pansi koma kulimbikira ntchito za mmunda monga kupalira kuti mbewu zisamalimbirane chakudya ndi udzu. Iye adati mbewu zokulira mtchire zimanyozoloka ndipo sizibereka bwino ngakhale mlimi ataononga ndalama zambiri kugulira feteleza. Omwe chimanga chawo chatuluka, ino ndiye nthawi yoyamba kulingalira kupalira ndipo chikafika mmawondo ndi nthawi yothira feteleza wina ndi kubandira kuti chinyamuke ndi mphamvu, adatero Lipita. Iye adati chimanga chikanyamuka ndi mphamvu maberekedwe ake amakhala osiririka ndipo mbewu yake ikakhala yabwinonso, phesi limodzi limabereka chiwiri kapena chitatu podzakolola nkudzakhala ngati minda iwiri pomwe udali umodzi. ",4 "Anthu Anayi Aperekera Umboni pa Mlandu wa Chamthunya Mboni zinayi za mbali ya boma zaperekera umboni wawo pa mlandu omwe a Misonzi Chanthunya akuganiziridwa kuti anapha bwenzi lawo Linda Gasa mchaka cha 2010. Mboni zitatu zinachokera ku Monkey bay komwe kuli cottage ya a Chanthunya ndipo mboni imodzi ndiyochokera ku ofesi ya boma yoona zolowa ndi kutuluka mdziko muno ya Immigration. Malinga ndi lawyer oyimira boma Dr. Steve Kayuni, mbonizi zilipo zisanu ndi imodzi ndipo pali chiyembekezo choti mbonizi zikhala zikupitilira kubwera ku bwaloli kudzapereka umboni wawo. Mmodzi anali ogwira ntchito kwa oyimbidwa mlandu komanso ena anali ogwira ntchitoku immigration. Mboni zinazo sizinabwere chifukwa amagwira ntchito koma lachinayi masana adzapezeka kuti adzayikire umboni, anatero Dr. Kayuni. Polankhulapo ku mbali ya ozengedwa mlandu a Micheal Goba Chipeta ati sangayankhulepo zambiri chifukwa mlanduwu udakali mkati. ",14 " Kudali kukwaya ku Mtima Woyera Udali ulendo wokhetsa thukuta lowopsa kuti zonse zilongosoke pakati pa Gray Lizimba ndi Iness Chimombo koma zonse zidafika pampondachimera Loweruka lapitali pomwe awiriwa adapatsana malonjezano omaliza. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Inde, pamtendere ndi pamavuto, moyo wabwino kapena matenda sadzasiyana. Awa ndiwo adali malonjezo pakati pa Gray ndi Iness omwe amachokera ku Bembeke mboma la Dedza ndipo onse amachita bizinesi mumzinda wa Lilongwe komanso amayimbira limodzi kwaya ku Mtima Woyera Parish ya mpingo wa Katolika mumzinda wa Lilongwe. Gray akuti ulendo udayamba mchaka cha 2009 awiriwa atakumana kutchalitchi ndipo Gray sadafune kuchedwa koma kufunsira pomwepo koma akuti sizidayende. Adandiyankha kuti ndisadzayerekeze kumulankhulanso za nkhaniyo, koma sindikadakwanitsa kutero. Mtima wanga udali pa iye ndipo ndidapitiriza kutchetcherera mpaka mu April, 2012 mpomwe adandilola, adatero Gray. Gray ndi Iness kupsopsonana patsikulo Iye adati atangomva mawu oti ndavomera adamva ngati wanyamula dziko lonse mmanja mwake, mtima ukudumphadumpha uku mmasaya muli chimwemwe chokhachokha. Iye akuti adakhala pachibwenzi mpaka mchaka cha 2014 mwezi wa November pomwe awiriwa adapanga malonjezano oyamba pachinkhonswe ndipo adagwirizana kukhala zaka zina ziwiri asadapange ukwati kuti akonzekere mokwanira. Kuchoka apo tinkakonzekera ukwati wathu ndipo tonse tidaikapo mtima mpakana zonse zidatheka pa 4 June, 2016. Tidakadalitsira ku Mtima Woyera ndipo madyerero adali kubwalo la St Peters Anglican ku Lilongwe, adatero Gray. Iye akuti Iness ndi chimwemwe komanso ufulu wake chifukwa amamulimbikitsa mzinthu zambiri ndi kumuthandiza mmaganizo pomwe mutu waima. Iness sadafune kunena zambiri koma kungotsimikiza kuti iye ali ndi chimwemswe kuti mtunda womwe adauyamba zaka 7 zapitazo wafika pampondachimera. ",13 "Ghana Igulira Apolisi Mifuti Wolemba: Thokozani Chapola /08/ghana-police.jpg"" alt="""" width=""550"" height=""366"" />Alandira mifuti ndi ma bullet proof-Ghana Police Boma la dziko la Ghana lati lipereka mifuti kwa apolisi onse ogwira ntchito za pansewu (Traffic) kutsatira ziwembu zomwe apolisiwo akuchitidwa. Malipoti a wailesi ya BBC ati apolisi asanu anaphedwa mwezi watha komanso ena awiri aphedwa lachitatu lapitali pamene zifwamba zina zinawombera apolisiwa pamene zimakana kuyimitsa galimoto yawo, zitayimitsidwa ndi achitetezowa. Padakalipano boma la dzikolo lati laganiza zogulira apolisi malaya omwe amateteza anthu ku chipolopolo cha mfuti (Bullet Proof) komanso kupereka mifuti ndi zida zina kwa apolisiwa. Nduna yoona za mdziko Ambrose Dery yati zida zatsopanozi zithandiza apolisi kulimbana ndi zauchifwamba zomwe zikuchitika mdzikolo komanso kudziteteza okha. ",7 "Kutetedza Okalamba ndi Udindo wa Aliyense MANEPO Wolemba: Thokozani Chiwaya Bungwe lolimbikisa ufulu wa anthu okalamba dziko muno la Malawi Network of Elderly Persons Organisation (MANEPO) lero lapempha anthu komanso mabungwe dziko muno kuti agwirane manja pothana ndi nkhaza zomwe anthu okalamba amakumana nazo dziko. Polankhulapo mu mzinda wa Blantyre, pambuyo maphuziro omwe bungwe la MANEPO linakonzera ma komiti a madera olandira madandaulo kuchokera kwa anthu okalamba omwe akuwatcha complaints response mechanism pachingelezi, mmodzi mwa akuluakulu ku bungweli a Louisa Kanyongolo ati maphuzirowa athandiza bungweli kufikira okalamba omwe akhuzidwa ndi nkhanza zosiyanasiyana ku madera kwawo komweko kuzela ku makomiti a pansi pa bungweli. Mamembala a komiti za MANEPO kulandira maphunziro Anthu amene ali mmakomiti abungweli omwe ali madera akufunika maphunziro ngati amenewa pofuna kusula kagwiridwe kawo ka ntchito pothandiza okalamba, anatero a Kanyongolo. Mai Louisa anatipitiliza kunena kuti makomitiwa ndi amenenso ali ndi kuthukera kofikira zosowa za anthu okalamba kamba koti ndi omwe amakhala nawo okolambawa kumidzi komweko. Mai Kanyongolo apempha mzika za dziko lino kuti zigwirane manja poteteza komanso kumenyera ufulu wa anthu okolamba pozindikila kuti tonse tizakalamba ndithu. Tonsefe tizakalamba ndithu choncho tizizindikira kuti ndi udindo wa aliyense wotetedza okalamba posayanganira ntsikhu wake, anaonjezera motero mai Louisa. Mau ake mmodzi mwa anthu amene anatenga nawo gawo pa maphuzirowa a Peter Mambala, anati maphuzirowa awathandiza kudziwa pamene amasalira pakagwiridwe kawo ka ntchito makamaka pofikila okalamba. Taziwa malire anthu komanso udindo wathu poteteza achikulire mdziko muno makamaka madera athu owenso ndikumene kukupezeka okalamba, anatero a Mambala. Mwadzina a Mambala anathokoza bungwe la MANEPO kamba kamaphunzirowa ponena kuti ntchito za mabungwe zimayenda bwino ngati anthu amenenso bungwelo likuwafikila ali nawo limodzi ngati momwe bungwe la MANEPO lachitila. Ntchito za mabungwe zimakanika kufikira cholinga chake cheni cheni ngati anthu akumudzi eni ake sakuyikidwamo kudzera ku makomiti ngati athuwa, anaonjedzera motero a Mambala. Maphuzirowa anakwanitsa kubweretsa pamodzi ma komiti a bungweli omwe amapezeka mboma la Blantyre. ",14 "Zikavuta, nawo anthu amakoka ngolo Ngolo imakokedwa ndi ngombe kapena abulu, koma pena zikavuta nawo anthu amakoka. Pachithunzipa, anyamatawa adakoka ngoloyi ngombe zitathawa. Nanga titani? Kodi ngoloyi ena satibera? Iwo adangoganiza zoyamba kukoka ulendo nayo pakhomo. Zikavuta zilibe dolo. ",10 " Kulingalira malumbiro Abale anzanga, tidakhala pa Wenela kuonera kulumbiritsa kwa atsogoleri. Woyamba kulumbiritsidwa adali Adama Barrow wa ku Gambia. Musandifunse kuti ameneyu ndidamudziwa bwanji, chifukwa sindikuyankhani. Mumafuna mumudziwe nokha? Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mwinatu sindidanene. Gambia ndi dziko limene anthu ake adachokera ku Zambia, muja anthu a ku Malawi adachokera ku Malaysia ndipo a ku Austria adachokera ku Australia! Ndife amodzi. Tsonotu Barrow adalumbilitsidwa kuofesi ya kazembe wa Gambia ku Senegal patatha sabata zingapo atakwapula mkulu uja Yahaya Jammeh pachisankho. Bolatu kwa anzathu amakhala sabata zingapo wina asanalumbire koma pano pa Wenela usiku siudutsa! Mwaiwala kale muja Moya Pete adalumbirira? Uyu Barrow adalumbira ku Senegal paja chifukwa Yahaya amakana kuchoka pampando. Demokalase ndiye imeneyo! Yaponda yamwa! Yalakwa yalakwa! Yahaya adaziona. Tsono sindikamba za kulumbira mdziko la eni. Kodi pa Wenela wina atakana kuti sanapambane pachisankho, wosankhidwa angakalumbire ku Mpanyira patsidya pa Tsangano? Zingatheke wosankhidwa pa Wenela kukalumbira ku Mbeya kapena Masvingo chifukwa sizingatheke pabwalo la pa Wenela? Winatu amalumbira adali mkulu uja Donal J Trump. Pajatu K2 000 ikutchedwa Trump chifukwa cha kukula mtima kwake. Iyetu adalumbira atagwira mabaibulo awiri. Loyamba lidali la mkulu wamtali uja, Abraham Lincoln. Kukadakhala kuno, bwenzi tikuti Moya Pete adalumbira atagwira baibulo lija adalumbirira gogo uja adandipeza ndikulima kwathu kwa Kanduku. Koma zingatheke? Ndipo popita kokalumbira, Trump adayamba wamwa tiyi ndi uyu akutulukayu, Barrack Obama. Kenako, onse adakwera galimoto imodzi. Kuno kwathu zingatheke? Abiti Patuma ndi Moya Pete kukwera galomoto limodzi? Tsonotu sindili pano kukamba za Barrow kapena Trump. Yanga nkhani ndi ya Saulo Chagalauza. Pajatu mkuluyo adabwera ndi moto, kukamba zosintha zinthu kuphiri. Mkuluyu lero wangoti ziiii! Sakukambapo kanthu za Joloji Mmera Chadyaka mkulu amene wafufuta chimanga chopezeka pambendera ya Dizilo Petulo Palibe, adatero Abiti Patuma. Palibe chimene ndidatolapo. Komatu Chadyaka adya ndalama zambiri. Nanga umboni wakuti adanyambita khusa uli kuti? adafunsa Gervazzio, akuika nyimbo ya Lucius Banda: Mabala. Malume ndalama kubisa kubanki Pamene Mbumba yawo ikufa ndi njala Adya ndalama bwanji? Zonsetu tiziona mwezi uno ukamatha chifukwa ndiye tsikulo kuli kokakatula ndi sizala, adatero Abiti Patuma. Adandipindanso. Chomwe ndikunena, uyu Saulo akupenya, akumva ndipo pakamwa ali napo koma sakulankhula. Watsamwa. Mwinatu akuopa Chadyaka paja mpandowu ngolimbirana. Ndani safuna kukhala Barrow kapena Trump? 2019 ndi chaka chinacho, adatero Abiti Patuma. ",10 " Kusowa kwa mpikisano nkwachabe Pali mantha kuti zipani za mdziko muno zingayoyoke ngati makatani ngati mipando yonona yachipani monga wa pulezidenti ndi wachiwiri wake ipitirire kukhala yongotola popanda wopikisana naye ku misonkhano yaikulu ya zipani. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Izi zaunikidwa ndi otsogolera zitukuko kumidzi ena ndi katswiri pandale potsatira zochitika kumsonkhano waukulu wa chipani cha Peoples Party (PP) komwe mpando wa pulezidenti ndi wachiwiri wake kuchigawo cha kumpoto padalibe kupikisana. Kusapezeka opikisana mmipandoyo kudapereka danga kuti mwini chipanichi, yemwenso ndi mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda adutse popanda omugwedeza. Naye wachiwiri kwa Banda, Khumbo Kachali adadutsa moyera. Mboma lomwe langopita kumene la DPP, mwini chipanicho komanso yemwe adaali pulezidenti, Bingu wa Mutharika samachititsa msonkhano waukuluwu nkomwe, mmalo mwake iye amangoloza anthu mmaudindo a mchipanicho. Chitsanzo, Mutharika adaloza Hetherwick Ntaba kukhala mneneri wachipani. Mtsogoleri wakale yemwenso adali pulezidenti mchipani cha UDF, Bakili Muluzi atangotula udindo kwa Friday Jumbe kudali kukokanakokana mpaka pano pomwe chipanichi chagawikana. Zitadziwika kuti kukhala msonkhano waukulu kuchipani cha PP, anthu ena monga mkulu wina wa bizinesi, Caesar Fatch, adabwera poyera kuti adzapikisana ndi Banda. Koma poyandikira chisankhocho, Fatch adalengeza kuti wazisiya, ati adzayeseranso kutsogoloku. Malinga ndi operekera ndemangawa, izi ndizo zikuchititsa kuti zipani za mdziko muno zizisokonekera pomwe pulezidenti wachipanicho wachoka paudindo chifukwa ofuna mpandowo amakhala akukokana, ena nkumathiothoka mchipani. Katswiri wa pa zandale, Blessings Chinsinga wati zipanizi zitamakhala ndi msonkhanowu nkupezekanso olimbirana nawo mmaudindo onse, achipani si bwezi mavuto omwe adachitika ku UDF ndi DPP atachitika. Izi si zachilendo mdziko; ngakhale mmaiko akunja mavutowa alipo. Koma mathero a zonse, chipani chimatha chifukwa anthu amayamba kukokana pomwe pulezidentiyo wachoka pampando. Ndibwino mipandoyi idziphangiridwa chifukwa pomwe pulezidenti wachoka, amene adayamba kupikisana naye ndiwo amakhala patsogolo, adatero Chinsinga. Makiyi Matukuta, mkulu wa bungwe la Malawi Carer ku Mayani mboma la Dedza, wati anthu kumeneko adali odabwa kumva kuti Banda wadutsa pampando wa pulezidenti popanda opikisana naye. Padzikhala kupikisana; anthu amakhala ndi chidwi kumva zomwe opikisanawo akonza. Zateremu ndiye kuti ufune usafune mtsogoleri wanu amakhala yemwe wadutsayo. Izi zimapha chidwi cha anthu ena omwe amafuna adzasankhe mtsogoleri yemwe amukonda, adatero Matukuta. ",2 " Mlonda anjatidwa kaamba kosolola Pamene kampani ya Inovantis mboma la Machinga imanyadira kuti izigona tulo tozuna chifukwa yalemba ntchito Ibrahim Justin, wa zaka 23, ngati mlonda woteteza katundu wawo ku ndipsi, kampaniyi sinadziwe kuti yatuma galu kumalondera nyama ya mbuzi yowotcha kale. Wapolisi wotengera milandu kukhothi pa Liwonde Police Post, Ezekiel Kalunga, adauza bwalo la milandu la Liwonde kuti pa April 19 chaka chino akuluakulu a kampani ya Inovantis adakagwada kupolisi kukadandaula kuti chipangizo chopanga mphamvu ya magetsi kuchokera kudzuwa (solar panel) chidasowa pakampanipo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Kafukufuku woyangana chipangizochi ali mkati mkulu wa alonda pakampanipo adakumana ndi munthu wina atanyamula chipangizocho, chimene adachizindikira kuti ndi cha kampani yawo. Alonda onse adatengeredwa kupolisi ndipo atapanikizidwa ndi mafunso kuti adazembetsa chipangizocho ndani, Justin adavomera kuti ndiyeyo adasolola. Kalunga adapempha khothi kuti limuthyape Justin ndi chilango chachikulu popeza khalidwe lakelo ndi lothawitsa anthu, makamaka a maiko akunja monga Inovantis, kudzakhazikitsa bizinesi zawo mdziko muno. Popereka dandaulo, Justin adapempha bwalo kuti limupatse chilango chochepa popeza iye ndi nsanamira ya banja lake. Woweruza milandu, Esther Phiri, adagwirizana ndi Kalunga ponena kuti khaliwe lakuba limabwezeretsa chitukuko mmbuyo kotero adamugamula kuti mlondayo akaseweze ndende kwa zaka ziwiri akugwira ntchito yakalavulagaga. Justin amachokera mmudzi wa Kaudzu mdera la mfumu yaikulu Sitola mbomalo. ",7 " Mwapasa achokeHRDC Zipani za Malawi Congress Party (MCP) ndi UTM Party zati ziunika mwakuya ganizo la mgwirizano wa mabungwe omenyera ufulu wa anthu la Human Rights Defenders Coalition (HRDC) lomema aphungu kuti akakane Duncan Mwapasa kukhala mkulu wa apolisi. Mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika adasankha Mwapasa ngati ogwirizira mpandowo potsatira kupuma kwa yemwe adali paudindowo Rodney Jose yemwe wakwanitsa zaka zake zokapuma. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Ena akufuna kuti achoke: Mwapasa Mwapasa akugwirizira mpandowo kudikira kuti aphungu a Nyumba ya Malamulo akaunike mbiri ndi luntha lake pankhani za chitetezo nkuvomereza kapena kukana kuti mkuluyu akhale pampandowu. Izi zili choncho potsatira zomwe ndime 154 (2) ya Malamulo a dziko lino imanena pakasankhidwe ka mkulu wa apolisi. Pulezidenti akuyenera kusankha mkulu wa apolisi pogwiritsa ntchito mphamvu zake koma Nyumba ya Malamulo ili ndi mphamvu zounika wosankhidwayo nkumuvomereza kapena kukana. Akatero, komiti younika za kasankhidwe ka maudindo ya Public Appointments Committee (PAC) ikhoza kuunika kagwiridwe ntchito ka mkulu wa apolisiyo nthawi iliyonse, akutero malamulo. Koma wachiwiri kwa wapampando wa HRDC Gift Trapence adati akuona ngati Mwapasa sangatsogolere bwino apolisi chifukwa amaoneka kuti amagwirizana ndi chipani cholamula cha Democratic Progressive (DPP) kotero sangatsogolere apolisiwo. Iye adati pachifukwachi, bungwelo lakonza zomema aphungu a Nyumba ya Malamulo kuti asakamuvomere Mwapasa akamakumana podzakambirana za ndondomeko ya zachuma ya 2019/2020 mwezi wa mawa. Mwapasa ndi wa DPP kutanthauza kuti chilichonse amapanga nchokomera chipani cha DPP. Kukhala mkulu wa apolisi, ndiye kuti polisi isanduka chida cha DPP mmalo mokhala chida cha Amalawi, watero Trapence. Mwapasa adakana kulankhulapo pa nkhaniyi pocheza ndi nyuzipepala ya The Nation Lolemba HRDC itangolengeza ganizo lake pa msonkhano wa atolankhani. Mneneri wa MCP Maurice Munthali wati chipanicho chili nchikhulupiliro mwa aphungu ake kuti akaona zochita nthawiyo ikadzafika pomwe mneneri wa UTM Party Joseph Chidanti Malunga adati chipani chiona zochita HRDC ikachipeza. Poti iyi ndi nkhani ya ku Nyumba ya Malamulo, tiyisiya mmanja mwa aphungu athu omwe tili nawo chikhulupiliro chonse kuti akaunike Mwapasa mopanda mantha kapena kunyengereredwa. Nthawi yopatsirana maudindo patebulo idatha, adatero Munthali. Ndipo Malunga adati: Padakalipano sitinena zambiri koma a HRDC akatipeza nayo nkhaniyi tidzayilandira nkupanga chiganizo mozama kuti Amalawi asataye chikhulupiliro mwa ife. Katswiri pa ndale George Phiri wati ndondomeko yosankhira mkulu wapolisi ndi yomveka bwino ndiye ngati HRDC yaonapo vuto ndi Mwapasa, zili ndi iwo kutengera nkhawa zawo kwa aphungu. Pulezidenti wasankha, koma zonse zikutsalira aphungu ku Nyumba ya Malamulo. HRDC ikawapatse nkhawa zake ndipo aphunguwo akaona kuti akatani pa nkhawazo. Koma khulupilirani kuti ngati Mwapasa wasankhidwira ndale kapena mtundu, akavutika kudutsa, watero Phiri. Nyumba ya Malamuloyi ikakakana Mwapasa ndiye kuti akhala munthu wachiwiri kukanidwa ndi nyumbayo kukhala mkulu wa apolisi kutsatira kukanidwa kwa Mary Nangwale mu 2006 yemwe adasankhidwa ndi mtsogoleri wakale Bingu Wa Mutharika. Aphungu ataunika maiyo adaona kuti samakwanira kutsogolera nthambi ya apolisi ndipo adamukana nkuunikira kuti Mutharika asankhe munthu wina woti atsogolere nthambi ya apolisi. Mwapasa wakhalanso mdindo wachiwiri yemwe bungwe la HRDC silikufuna akhale pampando kutsatira wapampando wa bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) Jane Ansah yemwe pakali pano HRDC ikutsogolera zionetsero zoti atule pansi udindo wake. ",11 " Mkulu wa kunyumba ya chisoni agwidwa ndi ziwalo Abambo awiri omwe amagwira ntchito kunyumba yachisoni kuchipatala cha Kamuzu Central (KCH) akuzengedwa mlandu wodula maliseche a mtembo wa munthu wamwamuna omwe unali mnyumbayo poyembekezera kuti abale ake adzautenge. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mneneri wa polisi ya Lilongwe, Ramsy Mushani, watsimikiza za nkhaniyi ponena kuti aganiziridwawa, Lufeyo Mphimbi, wa zaka 54, ndi Samalani Jabu, wa zaka 58, adadula ziwalozo anthu ena atawauza kuti pali msika wa K8 miliyoni wa ziwalo za munthu wamwamuna. Mushani wati anthu omwe akuwaganizira kuti adapeza msikawo, Sebita Mwale, wa zaka 27, ndi Eric Mwandira, wa zaka 34, adalonjeza ogwira ntchito kunyumba yachisoniwo kuti malonda akatheka adzawapatsa theka la ndalamazo. Mushani wati apolisi adagwira ndi kumanga Mwale ndi Mwandira pamalo omwetsera mafuta a galimoto a Kaunda pamsewu wopita ku Mchinji atatsinidwa khutu ndi anthu ena kuti awiriwo adali ndi maliseche a munthu wamwamuna omwe amagulitsa. Atafunsidwa za ziwalozo iwo adaulula kuti adachita kupatsidwa ndi abambo Awiri, Mphimbi ndi Jabu, omwe amagwira ntchito kunyumba yachisoni ku KCH ndipo onse anayiwa adavomera kuti adatenga nawo gawo pankhaniyi, adatero Mushani. Iye adati Mwandira adapita kunyumba ya chisoniyo kukakumana ndi Mphimbi, yemwe ndi mnzake wakalekale, kukakambirana za nkhaniyo ndipo anthuwo adakambiranadi muofesi ya Jabu nkumvana. Atagwirizana za malipiro Mphimbi ndi Jabu adalowa mchipinda chosungiramo mitembo momwe adatulukamo ndi malisechewo nkuwapereka kwa Mwandira yemwe adatengana ndi Mwale kuti akagulitse koma anthu adatsina khutu apolisi msanga, adatero Mushani. Mwale ndi Mwandira akuwazenga mlandu wopezeka ndi ziwalo za munthu, zomwe zitsutsana ndi ndime 16 yokhudzana ndi thupi la munthu mmalamulo a dziko lino, pomwe Mphimbi ndi Jabu akuyankha mlandu wodula ziwalo za munthu wakufa kutsutsana ndi ndime 18 ndinso wopereka ziwalozo kuti zitsatsidwe malonda kutsutsana ndi ndime 16 (gawo B) la malamulo okhudza za thupi la munthu. Bwalo la milandu ku Lilongwe Lachiwiri lapitali lidakana kutulutsa anthu anayiwa pabelo chifukwa ati likuopa kuti akhoza kuthawa. Pogamula pempho la owayimira anayiwo pamlanduwo, Alemekezeke Mando ndi Chris Tukula, kuti apatsidwe belo, woweluza milandu kubwaloli magisitiriti Patrick Chirwa adati kupatsa belo anthuwo nkovuta chifukwa mlandu wawowo ndi woopsa. Ndili ndi mantha kwambiri paganizo lopatsa anthuwa belo chifukwa pali chiopsezo chakuti chilungamo chikhoza kusokonezeka komanso chikhulupiriro chomwe anthu ali nacho mubwalo lino chikhoza kuonongeka, adatero Chirwa. Mkulu wa chipatala cha KCH, Noordeen Alide, samapezeka pafoni yake yammanja kuti alankhuleko pankhaniyi makamaka mmene ntchito ya kunyumba yachisoniyo imayendera. Mphimbi amachokera mmudzi mwa Chipazi, T/A Msakambewa, ku Dowa ndipo Jabu amachokera mmudzi mwa Msimbi, T/A Masula, ku Lilongwe. Mwale kwawo ndi kwa Chipoza, T/A Santhe, ku Kasungu, pomwe Mwandira ngwa ku Mwazisi, kwa Themba la Mathemba Chikulamayembe ku Rumphi. ",15 "MEC Yayamba Kupereka Zotsatira Za Chisankho Zotsimikizika Bungwe loyendetsa chisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) layamba kutulutsa zotsatira zotsimikizika za chisankho cha president chomwe chachitika lachiwiri lapitali. Malingana ndi wapampando wa bungweli Justice Dr. Chifundo Kachale, pofika 10 koloko ya mmawa wa tsiku la lero, bungweli linali litalandira zotsatira za maboma 26. Kachale: Tili mkati mowunika zotsatirazi Mwa mabomawa anali atawunguza ndi kutsimikizira zotsatira za maboma anayi okha omwe ndi a Mulanje, Chiradzulu, Mwanza komanso Likoma. Padakalipano zotsatira zomwe zatsala kuti zitipeze kuno ndi za boma la Mzimba ndi Dowa. Komanso padakalipano tili mkati mowunika zotsatira za maboma 22 omwe afika kalewa ndipo tibweranso nthawi ina kuti tifotokozere mtundu wa Malawi za nkhaniyi, anatero Dr. Kachale. Mwazina Dr. Kachale ati ngakhale akazembe a mabungwe akunja sanabwere kudzawonelera chisankhochi, koma akulumikizana nawo ndi kuwadziwitsa mmene chisankhochi chikuyendera kudzera mwa anthu ena a mdziko muno omwe amagwira ntchito ndi mabungwewa. ",11 " Ulemu kwa Geoffrey Mwale Mkuluyo adali msilikali. Aliyense pa Wenela amamudziwa bwino. Akangoti waledzera, tsikulo ndiye kumakhala ndewu zafumbi. Akapanda kupeza womenyana naye pa Wenela, zonse zimakathera kwa mkazi wake. Tonse tikudziwa kuti samasiya ndalama za ndiwo pakhomo msirikaliyo. Mkazi amati akafunsa ndalama ya pakhomo, makofi. Akati anawa chakudya, kukunthidwa ngakhale ndi zitsulo. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Ukhoza kukachita ngakhale uhule upeze yodyetsa anawa, adali kutero msirikaliyo. Koma akangomva kuti mwamuna wina kumsika wamupatsa mkaziyo bonya waulere, nayenso ali pamoto. Adali wozunguza. Ngakhale kupita kutchalitchi adaleka kalekale. Ena ankamutcha Boko, ena akuti Isisi. Koma adali msirikali basi. Tsiku lina adautunga kuyambira mmawa mpaka usiku. Amachoka kumowako nthawi itangodutsa 10 koloko. Wapamalopo atafunsa kuti amulipire, adalandira zibakera. Atafika kunyumba, adapeza kalata ili pakhonde. Chigawenga msirikali woipitsa dzina la asirikali anzako, munthu wa nkhanza kuposa Satana. Wandizunza mokwanira, ndamanga ulendo wakwathu. Komabe ndakusiyira chakudya chimene anzako anagula. Ndatengedwa ndi anzakowo, munthu wopanda nzeru iwe. Kukhakhala mtima ngati wakwananda kapena msana wa fulu. Estere. Estere adali mkazi wa msirikaliyo. Adalowa mnyumba. Adafikira patebulo pomwe padali mbale ziwiri zovindikira. Adadziwiratu kuti mwinamo mudali nsima, mwinamo ndiwo. Kukhosi kudachita kuti dyokodyoko. Dovu lidati liyambe kuchucha. Adayamba wasamba mmanja. Nthawi yopemphera adalibe. Mtima udali kugunda. Adavundukula mbale yoyamba, mudali miyala itatu. Miyala, osati mitanda itatu! Adatsegula mbale yachiwiri. Mudali masamba awiri a gwafa osaphika nkomwe. Adali atathiridwa tomato ndi mchere. Msirikali adakwiya. Adayatsa fodya wamkulu amene ankasunga mujombo. Adayamba kukoka. Utsi sumatuluka nkomwe, amaupanirira. Amachita ngati akubanika. Atatha kusutako, adakhala pansi. Momwe adagonera sadadziwe! Adayamba kulota. Adalota kuti adali atamwalira. Adafika kumwamba, pampando wachifumu. Woweruza anthu abwino ndi oipa adamuuza mkuluyo kuti adamupatsa mwayi wolapa koma iye sadafune kulapa. Adamupulumutsa kungozi komanso matenda koma sadafune kulapa. Udali kukonda ndewu, kumenya mkazi ndi ana ako. Tsono ndikupatsa mwayi umodzi wobwerera kudziko lapansi. Subwerera ngati munthu. Sankha chinyama chimene ukufuna, adatero woweruzayo. Msirikali uja adayamba kudya mutu: Ndisanduke mkango? Ndikaphaphalitsa nyama zina zakutchire. Koma ayi, alenje akandipha chifukwa akufuna chikopa, mchira ndi matumbo anga. Ndisanduke njovu, nyama ndi anthu azikandiopa. Koma ayinso, mnyanga wanga ukandiphetsa! Nanjinanji kusanduka nyani ndiye sindikalimba. Akandipha kuopa kuwapatsira ebola. Pamapeto pake, adasankha kukhala kangaude. Choncho nditsetsereka kudziko nkukakhala mnyumba yogumuka zakazaka. Womulenga adamuuza: Chabwino, usanduka kangaude. Bwerera kudziko lapansi. Apa mpomwe mkulu uja adadziwa kuti tsopano azitulutsa ulusi muja achitira kangaude. Hmmmmm! Hmmmmm! adali kutero, uku akumva kuti ulusi ukutuluka ndipo iye akutsikira kudziko lapansi. Hmmmm! Hmmmmm! adapitiriza, ulusi ukutuluka. Posakhalitsa adayamba kuona dziko lapansi. Hmmmm! Hmmmmm! adatsikirabe, ulusi ukutuluka. Kenako adafika padziko lapansi. Adayangana kumwamba ndipo dzuwa lidamuthobwa mmaso. Apa mpamene msirikaliyo adadzidzimuka kutulo kwakeko. Poti atembenuke, adazindikira kuti wadzionongera. Abale anzanga, mwinatu sindidakuuzeni, msirikaliyo ndi mmodzi mwa asirikali amene adamenya mnyamata wina timu yawo itagonja pampira wa dolola umene udalipo pa Wenela. Mnyamatayo adatisiya momvetsa chisoni, ndipo pano msirikaliyo limodzi ndi anzakewo sakudziwika kumene ali. ",15 " Zaka 18 kwa mphunzitsi wochimwitsa mwana Mphunzitsi yemwe adachimwitsa mtsikana wasukulu wa zaka zosadutsa 16 komanso kumupatsa mankhwala ochotsera pathupi wapukusa mutu wopanda nyanga bwalo la milandu la majisitireti ku Mzuzu litagamula kuti akalangidwe kundende kwa zaka 18. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Apa nkutitu mbwaloli muli ziii pomwe majisitireti Gladys Gondwe amapereka chigamulo chake kwa Mtendere Phiri, wa zaka 31, wochokera ku Bembeke, T/A Kachindamoto mboma la Dedza, yemwe amaphunzitsa pasukulu ina ya pulaimale ku Ekwendeni mboma la Mzimba. Zidaonekeratu kuti mphunzitsiyu sadali wokonzeka kuti alandira chigamulo cha mtunduwu chifukwa majisitiretiyu asadafike mbwaloli, Phiri adamveka akufunsa apolisi omwe adali kumuyanganira ngati zingatheke kutuluka patsikuli. Apolisiwo adamuyankha momupatsa chikhulupiriro chonse kuti zikuoneka kuti zimuyendera ndipo akonzeke chifukwa patsikuli akagona pofewa kunyumba. Komatu zinthu sizidamuyendere chifukwa mmphindi zisanu zokha, majisitireti adali atapereka chigamulochi. Phiri adangoti zyoli mchitokosi cha bwaloli. Popereka chigamulo chake Lolemba, Gondwe adati Phiri akuyenera kuseweza zaka 16 ndi kugwira ntchito yakalavula gaga pogona ndi mtsikana wosakwana zaka 16, ndipo pamlandu wopereka mankhwala ochotsetsa mimba adampatsa zaka ziwiri zomwe ziyendere limodzi ndi za mlandu woyambawu. Iye adati wapereka chilango chokhwimachi pofuna kupereka phunziro kwa aphunzitsi ena omwe ali ndi khalidwe logonana ndi ana awo asukulu mmalo mowalimbikitsa pamaphunziro awo. ",7 " Kanduku achotsa mfumu Thambala: Ankandituma kutolera ndalama Kwathina ku Mwanza pamene T/A Kanduku wachotsa gulupu Thambala komanso kulamula ena awiri kuti alipe mbuzi. Bwanamkubwa wa bomalo Gift Rapozo watsimikiza za nkhaniyi ndipo wati anakumana ndi mbali ziwirizi Lachitatu msabatayi ndipo agwirizana kuti akumanenso zofufuza zina zikatheka. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Rapozo wati wayitanitsa kuti amve zokambirana zomwe zimachitika kufikira kuti mpaka Thambala agumulidwe pa mpando. Padali nkhani zingapo zomwe zikukambidwa kuti mpaka a Thambala achotsedwe ufumu komanso mafumuwa amakumana pomwe amakambirana zinthu zomwe zapherezera kuchotsedwako ndiye pakhala zokambirana zomwe akhala akuunikira pa nkhaniyi mmbuyomu nkhaniyi tisadayitengere pena, adatero Rapozo. Lachisanu lapitalo Thambala adauza Tamvani kuti Kanduku wamuchotsa ufumuwo chifukwa adakakhala nawo pamsonkhano wa mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda omwe udachitikira ku Chikhwawa. Msonkhanowo, omwe cholinga chake kudali kutsekulira ntchito za chitukuko kwa Gulupu Chibwalizo kwa T/A Chapananga udachitika pa 7 August chaka chino. Koma Kanduku wati ndizoonadi kuti Thambala wagumulidwa pampando koma wati ndi za ziii! kuti iye wachotsedwa pa mpando chifukwa chopezeka pamsonkhano wa pulezidenti ponena kuti sizikugwirizana. Iye wati Thambala wakhala akubera anthu ndalama mwachinyengo powauza kuti Kanduku ndiye wamutuma. Ugulupu ndidawapatsa ndine, zomwe achita ndi mlandu, mfumu imayenera kukhala ya chitsanzo chabwino osati kumabera anthu ake, ndichifukwa ndawachotsera ugulupuwo ndikuwasiira unyakwawa, adatero Kanduku yemwe adati wakweza mfumu ina kukhala gulupu. Koma Thambala wati pa 7 adaitanidwa kukakhala nawo pamsonkhanowo koma ngakhale amapita adasiya milandu ina yomwe imayenera izengedwe. Iye wati atabwerako adalandira kalata yomwe imachokera kubwalo la Inkosi Kanduku kuti akufunika kubwalo lawo. Kumeneko kudali nkhani yokhudza malo yomwe ndidazenga ndiye munthu amene ndidamuzengayo samakhutira ndi chigamulo changa kotero adakagwada kwa Inkosi. Tili pabwalo kukamba za nkhaniyo ndi pamene ndidafunsidwa chifukwa chomwe ndimapitira ku msonkhano wa Pulezidenti kusiya nkhaniyo pambuyo. Apa adandichotsa ufumu ndipo adati ugulupu wanga waperekedwa kwa nyakwawa Lupiya. Magulupu ena monga gulupu Tulonkhondo ndi Ngadziwe adawalipitsa mbuzi, adatero Thambala movomerezana ndi mkazi wake. Iye wati atamva kuti ufumu wake wagumulidwa adalembera Rapozo kalata yomudandaulira. Kalatayo yomwe yaonedwa ndi Tamvani idali ndi mutu woti Dandaulo lakutsitsidwa udindo ndi kulipiritsidwa chindapusa yomwe mkatimo idatchula zopozeka kwake pamsonkhano wa pulezidenti. Ndikukhulupirira kuti sadagwirizane ndi kupezeka kwanga pamsonkhanowo, adatero Thambala. Koma Kanduku wati ndikutheka kuti Thambala akubweretsa dala nkhani yokapezeka kumsonkhano wa pulezidenti kuti ufumu wake uthenso. Iwo akhala akunamiza anthu kuti alamulidwa ndi ine kuti atolere ndalama kwa anthu. Anthu omwe akhala akundidandaulira anabwera kwa ine kundifunsa zomwe ndidakana. Adatolera ndalama zoposa K70 000, adatero Kanduku. Iye adati adaitanitsa Thambala kumufunsa za nkhaniyo. Kanduku wati chifukwa Thambala adapezeka wolakwa adamuchotsa pampandowo. Ndapereka kale ugulupu kwa mfumu ina, poti nkhaniyi ili kwa DC ndiye tikamva momwe zilili, adatsindika Kanduku. Iye adati walipitsa mfumu Ngadziwe pazifukwa zina osati zokakhala nawo pamsonkhano wa pulezidenti. Titafunsa Thambala ngatidi adatenga ndalamazo iye adavomera kuti amatenga ndalamazo motumidwa ndi Kanduku. Adatiuza kuti popeza kudera lathu kukudutsa njanji ndiye alembetsa mayina a anthu amene adzalandire nawo chipepeso ngati njanji yadutsa pakhomo pako. A Kanduku adati nditolere ndalama kuti tikawathokoze, adatero Thambala. Iye adati poyamba adapititsa K200 000 ya mthumba mwake kuti asatolerenso ndalama kwa anthu koma Kanduku adakana ponena kuti yachepa. Kenaka ndi pamene ndimauza anthu kuti andithandize, sindidachite mwakufuna kwanga, adatero. Rapozo adati nkhanizi zafika kuofesi kwake ndipo chenicheni chidziwika zokambiranazo zimatheka. ",8 "Bande Walimbikitsa Aphungu Anzake Kuti Agwire Ntchito Ndi Boma Latsopano Phungu wa dera la kumvuma kwa mzinda wa Blantyre, John Bande walimbikitsa aphungu a madera osiyanasiyana mdziko muno kuti agwire ntchito limodzi ndi boma latsopano kuti madera awo atukuke mwamsanga. Bande walankhula izi ndi Radio Maria Malawi potsatira ntchito zosiyanasiyana zomwe boma likugwira mdera lake. Bande: Posachedwa tiyika tala Iye wati kulumizana kwabwino ndi boma lomwe linalipo kwathandiza kwambiri kulandira ntchito zosiyanasiyana pa miyezi isanu ndi umodzi yomwe wakhala akutumikira mderali ngakhale kuti kuti iye ndi phungu woyima payekha. Bande anati zimenezi zathandizira kusintha mawonekedwe a dera lake makamaka pa ntchito za chitukuko. Tithokoze Mulungu kuti kuno ku Blantyre City East misewu yathu ndi yabwino popeza tapala koma posachedwapa ina mwa misewu imeneyi izakhala ya tala, anatero a Bande. Iwo atsindikanso kuti akhala akugwira ntchito ndi boma latsopano lomwe likutsogoleredwa ndi Dr. Lazarus Chakwera kuti ntchito za chitukuko zomwe zinayamba ndi boma la chipani cha DPP mdelaro zipitilire ndi kupindulira anthu awo. ",11 "Bokoharam Idakasungabe Msungwana Wachikhristu Wolemba: Thokozani Chapola s/2019/09/boko-haram.jpg 303w"" sizes=""(max-width: 576px) 100vw, 576px"" />Zigawenga za Boko Haram Msungwana wina wa chikhristu amene anagwidwa ndi gulu la zauchifwamba la Boko Haram mchaka cha 2018 akuti ali moyo. Malingana ndi malipoti a Independent Catholic News msungwana-yu anamugwira mu February chaka chatha pamodzi ndi atsikana ena oposera dzana limodzi a pasukulu ina ya ukachenjede mdzikomo. Malipoti ati atsikana enawo anawatulutsa patangopita mwezi umodzi ati kamba koti anali a chisilamu, koma kuti msungwana-yu Leah Sharibu anamuuza kuti amutulutsa pokhapokha atavomera zosiya chikhristu ndi kulowa chisilamu koma kuti iye anakakamirabe chikhristu chake zomwe zinachititsa kuti asatuluke ku malo a zigawengazo. Padakalipano boma la dzikolo lauza atolankhani kuti msungwana-yu adakali ku malo a zigawengazi, koma kuti likuchita zokambirana kuti zigawengazo zitulutse msungwanayu. ",13 " Anthu a ku Likoma alirira Ilala Anthu okhala pazilumba za Likoma ndi Chizumulu ati akulira ndipo moyo ukutentha chifukwa cha kusiya kuyenda kwa sitima ya Ilala. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC T/A Mkumpha wa ku Likoma yati kuleka kuyenda kwa sitimayo kwachititsa miyoyo ya anthu pa zilumbazo kukhala yovuta. Malinga ndi iye, kuonongeka kwa sitimayo kwachititsa chiyembekezo chimene anthuwo adali nacho kwa miyezi 10 pomwe sitimayo imakozedwa kuti chilowe mmadzi akuya. Moyo ukuvuta pa Likoma chifukwa sitimayo si ikuyenda. Ntchito za chitukuko zaimiratu chifukwa cha vuto la mayendedwe, adatero Mkumpha. Sitimayo idafa sabata zitatu zapitazo chifukwa cha mavuto ena. Izi zidachitika sitimayo itangoyenda maola ochepa, patatha miyezi 10 akuikonza. Kukonzako kudadya US$2 miliyoni (zoposa K800 miliyoni). Mneneri wa kampani yoyendetsa sitimayi ya Malawi Shipping Company adati ayambanso kuikonza zitsulo zina zikafika mdziko muno. Tikuyembekeza zitsulo zimene kampani ya Barloworld ipeze ndipo sitimayi iyambanso kuyenda ikangokonzedwa, adatero Msowoya. Iye adati zonse zikayenda, sitimayi ayamba kuikonza Lolemba. Aliyense ndi wokhudzidwa ndi momwe zinthu zilili. Ngakhalenso amene amabweretsa zitsulo zikuwakhudza koma tikuchita zotheka kuti sitimayi iyambenso kuyenda, adatero Msowoya. Ilala ndi sitima yokhayo yaikulu imene imayenda panyanja ya Malawi. Sitimayi idayamba kuyenda panyanjayo mchaka cha 1951 ndipo imanyamula anthu oposa 300. ",17 " Kasanthuleni za chisankho Pamene aphungu a Nyumba ya Malamulo akukonzekera kukumana kuyambira Lolemba likudzali, akadaulo ena awapempha kuti akalunjike pa za chisankho cha 2019. Ngakhale aphunguwo akhale akukambirana za momwe ndondomeko ya zachuma yayendera katswiri pa ndale George Phiri yemwe amaphunzitsa ku University of Livingstonia (Unilia) wati nkhani zina zonse zikhoza kuyamba zaima koma nkhani ya chisankho njofunika kuikambirana chifukwa ikukhudza tsogolo la dziko. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Aphungu mNyumba ya Malamulo mmbuyomu Zipani za ndale zakhala zikuthirira ndemanga pa za kalembetsedwe konyentchera mkaundula wachisankho, nkhani zokhudza zipolowe pa ndale, kusowa kwa makina akalembera ndi mphekesera zofuna kudzabera chisankho ndipo Phiri wati uwu ndi mpata woti aphungu akakambirane nkhanizi mwachindunji. Nkhani ya bajeti ili apo, aphungu asakataye nthawi ndi za ziii ngati momwe amachitira muja. Nthawi yatha, uwu ndi mwayi wawo wokonza Malawi. Kukonza Malawi ndi chisankho chomwe chikubwerachi, adatero Phiri. Iye adati nkofunikanso kuti aphungu asanthule bwino za momwe akhala akuyendetsera thumba la ndalama za chitukuko la Constituency Development Fund (CDF). Ndemangayo ikudza pomwe lipoti ya nduna ya zachuma Goodall Gondwe kumayambiriro a chaka chino lidaonetsa kuti aphungu 20 adasokoneza ndalama za CDF koma mpaka lero palibe phungu amene adatchulidwa ndi kusololako. Phungu aliyense amalandira K18 miliyoni mu bajeti iliyonse koma apanga nayo chiyani cholozeka? Anthu akuvutikabe ngati kale, watero Phiri. Katswiri pa za kayendetsedwe ka dziko Makhumbo Munthali wati aphungu ayenera kukambirana za momwe chisankho chingayendere mwa bata ndi chilungamo. Iye adati pali nkhani zingapo zimene a zipani akhala akudandaula monga kalembera wa zisankho wophotchoka, kusowa kwa makina ku bungwe la zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) zomwe zidadzetsa chikaiko zimene aphungu akuyenera kukaunikira. Pambali pokambirana mfundo zoti chisankho chidzakhale cha mtendere ndi chilungamo, akumbukirenso nkhani zina monga mabilu okhudza zachuma monga za migodi. Ndalama zankhaninkhani zikutuluka mdziko muno chifukwa chopanda mfundo zokhwima, watero Munthali. Chipani cha Peoples P(PP) chati chikugwirizana ndi maganizo a anthu ndi akadaulo pa nkhani zofunika ku nkhumano ya aphungu. Mneneri wachipanichi Ackson Kalaile wati nkhani ya chisankho njosathawika pafikapa chifukwa ikukhudza miyoyo ya aMalawi. Tafika pano Amalawi adataya chikhulupiliro ndiye ntchito yonse yobwezeretsa chikhulupilirocho ili mmanja mwa aphungu ndipo nthawi yake ndiyomweyi, adatero Kalaile. Mneneri wa Malawi Congress Party (MCP) Maurice Munthali adati akuluakulu achipanichi ndi aphungu ake akumana mawa Lamulungu kuomba mkota wa mfundo zopita nazo kunyumbayi. Mneneri wachipani cha Democratic Progressive (DPP) Nicholas Daus adati chipanicho sichingakambe mfundo zake ndi atolankhani chifukwa zopita kunyumba yamalamulo zili ndi njira yake yodzera. Iye adati zonse zikakonzeka, komiti yoyenera idzalengeza. Sitingamakambirane ndi atolankhani mfundo zomwe takambirana choncho ndilibe yankho, adatero Dausi Posanthula nkhani ya momwe aphungu agwirira ntchito mmbuyomu, iye adayamika momwe aphunguwo adatsatira nkhani yomwe nduna yakale ya malimidwe George Chaponda amamuganizira kuti adachita chinyengo pogula chimanga kuchoka ku Zambia. Iye adati ngakhale izi zili choncho, aphungu amene adasankhidwa mu 2014-wa akanika mzambiri chifukwa mmalo mothandiza kutukula dziko, iwo adathandizira kulilowetsa pansi. Aphungu adayesetsa kukoka nkhaniyo ya chimanga ndipo tidayamika, koma tikawayika pasikelo ya udindo wawo, palibe chomwe adachitapo mzaka zonsezi, adatero Munthali Amalawi ena amene tidacheza nawo aonetsa kuti khumbo lawo lagona poti aphungu akambirane zakupsa zokhudza chisankho. Jane Mapira wa ku Lilongwe wati iye akadakonda aphungu akadakambirana nkhani yokhudza kusintha akuluakulu a MEC omwe wati akhumudwitsa kale anthu nzochitika zawo. Wilson Thomas wa ku Zomba wati iye sakuona choti aphungu azikatayira nthawi nkukambirana zinthu zomwe sizingasinthe kalikonse ndipo wati kuli bwino aphungu akangokambirana za bajeti nkumabwerako. Ngakhale atakambirana nkhani za chisankho, palibe chingasinthe chifukwa nthawi yatha kale. Apa akangokambirana za bajeti nkumabwerako kukadikira chipande mu May chaka cha mawachi basi, watero Thomas. Ukatha msonkhano wa aphungu wa chaka chino, aphunguwo adzaakumana komaliza mwezi wa March chaka cha mawa, kutangotsala miyezi iwiri kuti chisankho cha 2019 chichitike. ",11 " Zilango zophweka zivulaza maalubino Miyezi 18 kwa ofuna kugulitsa alubino ku DZ Pali mantha kuti maalubino angapitirire kuona zokhoma mdziko muno ngati boma silichita machawi kuti lamulo latsopano loteteza anthuwa liyambe kugwira ntchito, mkulu wa bungwe lomenyera ufulu wa maalubino la Association of People with Albinism in Malawi (Apam), Bonface Massah, watero. Mantha a mkuluyu akudza pamene anthu amene apezeka olakwa pozunza kapena kusowetsa maalubino akupitirira kulandira zilango zozizira. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Lachisanu sabata yatha, bwalo la milandu mboma la Dedza lidagamula mayi Siyireni Nyata ndi Chrissie Lajabu kukaseweza kundende zaka ziwiri ndi miyezi 6 poopseza mwana wa zaka 14 kuti amupezera kale msika. Malinga ndi mneneri wa polisi ku Dedza, Edward Kabango, amayiwa akhala akulankhula izi kwa nthawi yaitali. Amati ndi kanyama kosendasenda ndipo akapezera kale msika woti akakagulitse, adatero Kabango. Kaamba ka kuopsezedwako, mwanayo akuti adasiya sukulu pochita mantha kuti angakumane ndi anthu amene amati amugulawo. Makolo a mwanayu akuti adakadziwitsa apolisi ndipo pa April 15 amayi awiriwo adanjatidwa. Bwalo lidawapeza olakwa ndipo lidawaimba mlandu wobweretsa mantha kwa mwanayu ndipo adawalamula kuti akaseweze zaka ziwiri ndi miyezi 6 kundende. Chilangocho chikudza pamene mkulu winaso ku Machinga, Sinoyo Wyson, wagamulidwa kuti akakhale kundende zaka ziwiri posowetsa mwana wa zaka 11 wachialubino. Mu May chaka chinonso amuna awiri ku Zomba adawalamula kukaseweza miyezi 12 popezeka ndi mafupa alubino. Massah akuti si zoona kuti milandu yotere izikhala ndi zilango zofewa ndipo wati bungwe lawo lichitapo kanthu kuti maalubino asamakhale mwamantha. Ndikumvanso kwa inu za nkhani ya ku Dedzayo, koma tifufuza. Pankhani ya ku Machinga ndiye tidakagwadanso kubwalo lalikulu kuti aunikenso chilangochi, adatero Massah. Koma iye adati oweruza milandu si olakwa pa zigamulo zomwe akuperekazi chifukwa malamulo a dziko lino amapereka zaka ziwiri kwa wopalamula mlandu wozembetsa munthu. Iye adati mavuto onsewa angathe ngati lamulo la Anti-Human Trafficking lingayambe kugwira ntchito. Lamuloli lidavomerezedwa kale ndi aphungu a Nyumba ya Malamulo komanso mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika. Lamulo latsopanoli likupereka zaka khumi kwa amene wapalamula mlandu wonga uwu, chomwe ndi chilango chokhwimirako. Tayesera kufunsa anzathu a boma nthawi yomwe lamuloli liyambe kugwira ntchito koma zomwe tikumva si zopereka chiyembekezo. Maalubino sakutetezedwa kupatula kungolankhula chabe, zomwe sizingateteze anthuwa, adatero Massah. Koma mneneri muunduna woona za chilungamo ndi malamulo, Apoche Itimu, akuti lamuloli lidavomerezedwa kale ndi Mutharika. Chomwe ndikudziwa nchakuti lamuloli lidavomerezedwa, sindingakumbuke kuti lidasindikizidwa liti. Panopa kwangotsala kuti liyambe kugwira ntchito, koma ngati mukufuna kudziwa zenizeni za lamuloli funsani unduna wa zamdziko, adatero Itimu pouza Tamvani. Mneneri ku unduna wa zamdziko, Rose Banda, Lachiwiri msabatayi adati timuimbire tsikulo lisadathe kuti atipatse zenizeni zokhudza lamuloli. Koma pakutha pa tsikulo Banda adati sadakumane ndi oyenerera amene angamufotokozere nkhani yonse yokhudza lamuloli. Lachitatu adatitumizira uthenga pafoni kuti akhala ndi zotsatira zonse pofika Lachinayi. Maiko monga Tanzania, Mozambique, South Africa ndi Zambia ali ndi lamuloli lomwe limakhaulitsa opezeka kuti apalamula mlanduwu, pamene mtsogoleri wa dziko la Zimbabwe Robert Mugabe adakhazikitsa ndondomeko yapadera yothanirana ndi anthuwa. Mutharika wakhala akumalankhula pawailesi ya MBC mawu oopseza kuti amene apezeke akusautsa maalubino athana nawo. Koma ngakhale Mutharika angalankhule maka, kukhoti akuyendera zomwe malamulo amanena posatengera mawu ake. Izi zapangitsa mabungwe monga Apam kuti alimbikitse kupempha boma kuti likhazikitse lamulo lokhwima pofuna kuteteza miyoyo ndi maufulu a maalubino. Massah akuti nthawi yakwana kuti mabungwe amene amamenyera ufulu wachibadwidwe ndi ena agwirane manja pofuna kuthana ndi mchitidwe wozunza maalubino. Mdziko muno mukangochitika nkhani mumaona amabungwe akubwera pamodzi kudzudzulapo, koma zomwe zikuchitika mmakhoti athu palibe amene akulankhulapo. Tikufunika tigwirane manja kulimbana ndi nkhaniyi ngati tikufuna tipambane nkhondo yoteteza anthu [amene ali ndi zilema monga maalubino], adatero Massah. Nkhani zosowetsa maalubino komanso kufukula manda awo zidafika pachimake mu February chaka chino ndipo anthuwa pamodzi ndi amabungwe ena adachititsa msonkhano mumzinda wa Blantyre kudandaulira boma kuti lichitepo kanthu. Pamsonkhanowo, Senior Chief Kawinga ya mboma la Machinga idati ndi zosamveka kuti chilango cha wosowetsa munthu chizikhala chochepa. Munthu wina adaba ngombe koma adamupatsa chilango choti akakhale kundende zaka zisanu pamene wosowetsa munthu akumupatsa zaka ziwiri. Pali chilungamo apa? Kodi ngombe ikhale yofunikira kwambiri kuposa munthu? Kodi alubino si munthu? adadandaula Kawinga. ",7 " Anatchezera Ukuchita njomba Gogo Natcheteza, Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndine mtsikana wa zaka 25 ndipo ndakhala pa chibwenzi ndi mnyamata wina kwa zaka zinayi. Mnyamatayu ali ndi nyumba yake ndipo akugwira ntchito yabwino pa kampani ina yopanga mafuta wophikira mu mzinda wa Lilongwe. Tidagwirizana kuti tidzakwatirana, koma mnzanga ndikamufunsa za banja amangozengereza. Kumuuza kuti abwere kwathu azaonekere amangoti ndidzabwerabe mpaka zaka nkumatha. Gogo, kodi pamenepa nditani popeza mnyamatayu ndimamukonda ndi mtima wanga wonse? JPJ Lilongwe JPJ Nkhaniyi siyachilendo. Atsikana ambiri amadandaula kuti anyamata adawauza kuti adzawakwatira, koma akuchulutsa njomba. Mnyamata wofuna banja sasowa. Sazengereza mwayi wokaonekera kwa makolo a mtsikana ukapezeka. Anyamata ambiri safuna banja. Amangofuna kugona ndi atsikana ndipo chakumtima kwawo chikapwa amawasiya nkukapeza ena. Uku nkulakwa. Muunikeni bwino bwenzi lanuyo kuopa kudzanongoneza bondo mtsogolo. Paja amati mtsinje wa tinkanena udakathera msiizi. Gogo Natchereza Mutu wazungulira Ndine mtsikana wa zaka 23 ndipo ndili ndi mwana mmodzi. Mnyamata wina adandiuza kuti akundifuna chibwenzi ndi cholinga choti adzandikwatire mtsogolo ndipo ndidalola. Koma makolo ndi abale ake amamukaniza kuti asakwatiwe ndi mtsikana wa mwana moti panopa zochita za bwenzi langa sindikuziona bwino. Ndikamuimbira foni nthawi zina sayankha. Ndikamutumizira uthenga pa WhatsApp umaonetsa kuti waona, koma sayankha. Gogo, mutu wanga wazungulira nditani? APA APA Usadandaule, ungozivomereza. Makolo ena amaletsa ana awo kukwatira atsikana oti adaberekapo kumene kuli kulakwa. Anthu akakondana saona zoti wina ali ndi mwana kapena ayi. Apa zikuonetsa kuti mnyamatayo wamvera zonena za makolo ake. Choncho kutha kukhala kovuta kuti chibwenzi chanu chipitirire. Limba mtima, mudzapeza mnyamata wokukondani posatengere kuti mudaberekapo. Usada nkhawa. Chachikulu ndi kudekha. Sunga khosi mkanda woyera udzavale. ",12 " Kulira, chimwemwe ndi banki mkhonde Ngakhale adali ndi chidwi choyamba bizinezi kuti atukuke, kusowa kwa mpamba kumapondereza khumbolo. Sanderson Yuba wa mmudzi mwa Namalima kwa T/A Nazombe mboma la Phalombe adakanika kutenga ngongole kubanki kaamba kosowa chikole komanso kuopa chiongola dzanja chokwera. Lero mkuluyu ndi mmodzi mwa makhumutcha mderalo kutsatira ngongole yomwe adatenga kubanki mkhonde ndi kuyamba bizinezi ya matabwa mpaka wamanga nyumba ya malata, kugula njinga ya moto ndi ziweto. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mabanki mkhonde afalikira mdziko muno Kupanda banki mkhonde loto langa loyamba bizineziyi si likanakwaniritsidwa. Bwenzi pano ndili mpopangolo wa mmudzi. Bankiyi idandithandiza kupeza mpamba, adatero Yuba. Yuba ndi mmodzi mwa Amalawi omwe miyoyo yawo yasintha chifukwa cha mabankiwa. Koma si onse otenga nawo mbali akusimba lokoma, ena akumana ndi zikhomo kutsatira kusokoneza ngongole zawo za banki mkhonde ndipo ali muumphawi. Mmodzi mwa iwo ndi Janet Mawata wa mboma la Phalombe lomwelo yemwe atakanika kubwenza ngongole ya K20 000 adalandidwa katundu. Mayi wina, yemwe anati tisamutchule dzina, ku Zomba adalandidwa nyumba kaamba ka ngongole ya K250 000 ndipo padakalipano umoyo wake ukuvuta. Pakutha pa chaka, mmizinda ndi mmatauni anthu akumagawana ndalama zochuluka, ena mpaka K7 miliyoni, kuchoka kubanki mkhonde. Koma ndalamazi zimasungidwa mnyumba mwa membala wosankhidwa kutero, osati kubanki. Izi zidachititsa mkulu wakale wa banki yaikulu mdziko muno ya Reserve Bank of Malawi (RBM), Charles Chuka kunena kuti mabanki mkhonde sakufunika chifukwa akusokoneza kayendedwe ka chuma. Mabungwe ena atsutsa izi. Mkulu wa Community Savings and Investing Promotion (Comsip) bungwe lomwe limayanganira mabanki mkhonde, Tenneson Gondwe, adati kutero ndi kusokoneza cholinga cha ndondomekoyi yomwe imapereka mpata wa ngongole kwa anthu osowa. Anthuwa amasonkha ndalama zomwe amabwerekana ndi kuyamba mabizinezi komanso kugawana pakutha pa chaka. Kulowerera kwa RBM kungasokoneza miyoyo ya anthu. Ngati akufuna angopanga banki ya kumudzi yomwe izikwaniritsa zosowa za anthu, adatero Gondwe. Kafukufuku wa bungwe la Finscope adapeza kuti anthu 50 pa 100 ali onse mdziko muno ali ndi kuthekera kofika ku mabanki a pamwamba koma 21 pa 100 wo ndi amene ali ndi mabuku ku mabankiwo. Zotsatirazi zikupereka mpata kumabanki mkhonde kukhala ndi anthu ochuluka poonjezera chiongola dzanja chochepa chomwe amapereka pa ngongole iliyonse. ",2 "Lamulo Lothandiza Anthu Kupeza Mauthenga Mosavuta Liyamba Kugwira Ntchito Posachedwa-Kazako Unduna wa zofalitsa nkhani watsimikizira aMalawi kuti lamulo lothandiza anthu kupeza mauthenga mosavuta la Access to Information (ATI) liyamba kugwira ntchito posachedwapa. Kazako: Anthu anavota kuti zinthu zisinthe Nduna mu undunawu a Gospel Kazako ndi omwe anena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi. Iwo ati mtsogoleri w adziko lino anasayinira kale lamuloli koma anthu ena mu ulamuliro wa chipani cha DPP ndi omwe amalepheretsa kuti lamulori liyambe kugwira ntchito yake. Vuto la dziko lomwe limayendetsedwa ndi mabanja awiri kapena atatu kapena anayi limakhala limeneli ndipo umboni wake ndiwa lamulo limeneli la Acces to Information. Nyumba ya malamulo inavomereza komanso a president anasayinira koma mabanja ena ake ochepa anangoganiza kuti lisayambe kugwira ntchito zomwe ndi zoyipa kwambiri, anatero a Kazako. Pamenepa a Kazako ati mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera waonetsa kale chidwi choti lamuloli liyambirenso kugwira ntchito ndipo wati boma lomwe lilipo padakalipano lilibe chilichonse choti libise choncho lamuloli liyamba kugwira ntchito. ",7 " Ntchito yomanga njanji ya ku Nkaya yaima Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Ntchito yomanga njanji yochoka ku Kachaso kupita ku Nkaya ayiimitsa mpaka kampani ya Mota-Engel ndi ogwira ntchito kukampaniyo atamvana chimodzi. Ogwira ntchitowo akunyanyala pofuna kukakamiza mabwana awo kuti awakwezere malipiro komanso kuti nzika 300 za ku Thailand zipakire. Kunyanyalaku kudayambira Lolemba pa 24 June ndipo Lachiwiri Nduna ya za Ntchito Eunice Makangala idatsetserekera kumeneko kukalankhula ndi ogwira ntchitowa kuti abwerere kuntchito koma izi sizidaphule kanthu chifukwa pofika Lachitatu mmawa nkuti ogwira ntchitowa asadabwerere kuntchito. Mmodzi mwa ogwira ntchito kumeneko ndipo akuchita nawo sitalakayo koma sadafune kutchulidwa dzina adauzaTamvaniLachitatu kuti iwo sagwira ntchito mpaka dandaulo lawo litamveka. Ndikukamba pano anzathu akubwera kuchokera ku Mwanza kudzatithandiza sitalakayi, sitibwerera kuntchito mpaka titaona malipiro athu akukwera komanso anthu omwe achoka mdziko la Thailand akubwerera kwawo, adatero mkuluyo. Padakhota nyani mchira mpakuti kampaniyi sabata zitatu zapita akuti inathotha gulu la ogwira ntchito kumeneko omwe ndi a mdziko muno ndi kulemba ena ochokera ku Thailand. Anthuwa akuti ndi pafupifupi 300 koma chenicheni chomwe amabwerera mdziko muno sichioneka chifukwa ena sadziwa ntchito ndipo amachita kuphunzitsidwa ndi Amalawi. Chodabwitsa nchakuti malipiro a akunjawo adali okwera kuposa a Amalawi omwe amatha ntchito. Ntchito yake yomwe akugwira ndi kuyendetsa mathirakitala ndi a mabewula zomwe Amalawi timatha, ena mwa alendowo sakuthanso kugwira ntchito ndipo tikuwaphunzitsa ndife. Tikudabwa kuti izi zikuchitika bwanji? Nanga nchifukwa chiyani akulandira ndalama zoposa ife omwe tikutha ntchito? adadabwa mkuluyo. Malinga ndi iye, Amalawi akulandira ndalama yosaposa K30 000 pomwe akamuna akunjawa akumatula makwacha owaposa iwo. Koma Makangala adati walankhula ndi akuluakulu a kampaniyi kuti mamulumuzana a mdziko la Thailand omwe alibe ukadaulo wa ntchito apakire ndipo azipita. Lolemba, mkulu wa kampaniyi Jose Denis da Silva wati akuluakulu a kampaniyi akukambiranabe ndi ogwira ntchitowa ndipo iye adapereka chiyembekezo kuti kusamvanaku kutha popanda zovuta. Mota-Engel ndi kampani yomwe yalemba kampani ya ku Brazil yotchedwa Vale kuti imange njanjiyi yomwe ikuchokera ku Moatize ku Tete mpaka ku Nacala Port mdziko la Mozambique kudutsira mdziko la Malawi. Malinga ndi yemwe amatitsina khuku pankhaniyi, pofika Lachinayi akuti mbali ziwirizi zinalepherabe kugwirizana ndipo zomwe auzana nkuti zokambirana zidzachitike Lachiwiri sabata ikudzayi. Izi zikusonyeza kuti sitigwira ntchito mpaka Lachiwiri lomwe tidzagwirizane mfundo zenizeni tisanabwerere ku ntchito. Pazokambiranazo akutinso kubwera akuluakulu ena a kampaniyi ochokera mmayiko ena komanso mbali ya boma. Sitikusinthika pa mfundo zathu kuti akuluakulu a dziko la Thailand azipita ndipo timva kuti pomwe tikumane Lachiwiriro atiuza zotani, adatero mkuluyo. Pomwe timalemba nkhaniyi nkuti yankho pa kunyanyalako lisanadziwike. Kampani ya Mota idalemba Amalawi oposa 3 000 omwe akugwira ntchito zosiyanasiyana kumeneko. ",17 " Wagolosale ndiye adandipatsa nambala yake Anthuni, njira zophera khoswe nzambiri koma chachikulu khosweyo afe basi. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ena pofuna mkazi amachita kugwa mngongole kuti aoneke ngati, komatu nkhani ya mnyamata wodziwika bwino pa zautolankhani, Vincent Phiri, yemwe sabata yathayi wapanga chinkhoswe ndi okondedwa wake Mable Pikani, sidakhale choncho. Mnyamatayu akuti kumangika pakamwa kudalipo mpaka adachita kufunsa nambala ya lamya pagolosale yomwe msungwanayo amakonda kugula zinthu ku Ndirande munzinda wa Blantyre komwe onse amakhala. Akufuna kudzakhala banja lachitsanzo: Mable ndi Vincent Iye adati ngakhale adatenga nambala ya lamyayo, sadayende moyera kufika pomwe alipa kaamba kakuti akatumiza timauthenga ta palamya namwaliyo amayankha mosonyeza kuti alibe chidwi. Koma pali khumbo, njira imakhalapo. Tsiku lina ndidaganiza zomuimbira ndipo ndidamupempha kuti ngati nkotheka tikumane ndili naye mawu ndipo adandiyankha kuti ngati ndikufuna kukumana naye ndikampeze kwawo, adatero Phiri. Iye adati posakhalitsa ubale udayambika mpakana kugwirizana za banja chifukwa onse adaona kuti kudalembedwa kuti adzakhalira limodzi mpaka imfa. Chinkhoswe chidalipo pa 28 November ku Kabula Hill mboma la Blantyre ndipo zokonzekera zili mkati kuti chaka chamawachi adzamange ukwati woyera. Vincent adati Mable ndi munthu yemwe ali ndi mtima wa mayi, wachikondi, wangwiro komanso wolimbikira ndi wodziwa chomwe akufuna mmoyo mwake. Naye Mable adati Vincent ndi mnyamata wolimbikira, wamasomphenya ndinso wopanda mtopola ndi anthu. Pano Vincent ndi woyanganira za momwe malonda akuyendera kukampani ya Finca ndipo akuchita maphunziro a zosunga ndi kubwereketsa ndalama, pomwe Mable ndi namandwa wokonza zovala ndipo ali ndi malo akeake osokeramo zovala. Koma onse awiriwa ndi atolankhani. Vincent amachokera mmudzi mwa Mkutumula kwa mfumu yaikulu Kwataine ku Ntcheu pomwe Mable amachokera mmudzi mwa Kwachama, mfumu yaikulu Khongoni ku Kasiya mboma la Lilongwe. ",15 " Alimbikitsa chitetezo cha okhala mmalire Covid-19 Bungwe la Farmers Union of Malawi (FUM) lati pakufunika kulimbikitsa chitetezo cha anthu mmadera akumidzi omwe ali mmalire a dziko lino ndi maiko ena pofuna kupewa kufala kwa matenda a Covid-19. Mlangizi wamkulu wa bungweli mboma la Mwanza Caswel Kachingwe adanena izi sabata latha pamwambo wopereka mabeseni, ndowa ndi sopo kumidzi ya kwa mfumu Nthache ndi Govati mbomalo polimbikitsa anthu kusamba mmanja ngati njira yopewera matendawa. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Nthache (Kumanzere) ndi Kwachingwe (Kumanja) kusamba mmanja pa mwambowo. Maderawa, omwe ali mmalire a dziko ndi la Mozambique ndi komwe bungwelo likuchitako pulojekiti yolimbikitsa kadyedwe kabwino. Nthendayi yavuta mmaiko oyandikana nawo ngati Mozambique. Anthu a kwa Nthache ndi Govati ayandikana ndi dzikoli moti akhonza kugwidwa ndi mliliwu ngati satetezedwa ndi kulimbikitsidwa kutsata njira zopewera. Tathandiza ndi zinthuzi ndipo tionetsetsa kuti zigwire ntchito popeza kupewa kumaposa kuchiza, adatero Kachingwe. Iye adati zipangizozi zikaikidwa mmalo omwe anthu amadutsa kwambiri ndi mokumanirana. Woona za umoyo mbomalo Ireen Zuze adavomerezana ndi Kachingwe pa zolimbikitsa chitetezo cha anthu mmaderawo. Zipangizo zothandiza anthu kupewa makamaka kuti azisamba mmanja ndi sopo pafupifupi zikufunika. Tikuthokoza FUM pothangatira ntchito yathu yolimbikitsa umoyo wabwino mboma lino, adatero Zuze. Mfumu Nthache idali yokondwa ndi kunena kuti ukhondo uyanja dera lake ndipo chitetezo ku Covid-19 chikula. ",6 " Fodya nkunazale Pamene alimi a fodya ali yakaliyakali kukonzekera ulimi wa 2015/16, mlangizi wa zaulimi wa fodya mboma la Rumphi, Charles Jere, walangiza alimi kuti atsatire ndondomeko ndi malangizo oyenera popanga nazale ya fodya pofuna kupindula ndi ulimi wawo. Pocheza ndi Uchikumbe posachedwapa, Jere adati nazale ya fodya si ili ngati ya ndiwo zamasamba kaamba koti imafuna chisamaliro chapadera chifukwa kupanda kutero palibe chimene mlimi wa fodya angapindule ndi fodya nchifukwa chake pali mawu akuti fodya nkunazale. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Choyamba mlimi akuyenera kupeza malo omwe aikepo nazale yake. Malowa akuyenera kukhala kufupi ndi madzi oyenda kapena omwe akuoneka opanda tizilombo toyambitsa matenda a mtundu wina ulionse, adatero Jere. Jere adati mlimi akuyenera kutipula nazale kutengera ndi kukula kwa munda wake. Mlangiziyu adati paekala imodzi bedi la nazale likuyenera kukhala lotalika mamita 30 ndi mita imodzi mlifupi pomwe hekitala imafunika mabedi atatu a muyezo woterewu. Akapanga bedi lija mlimi akuyenera kutenga mapesi a chimanga nkuwasanja pabedi lija ndipo akatero awaotche ndi cholinga chofuna kupha tizilombo tomwe tidali mudothi tomwe tikadatha kuononga fodya panazalepo. Apa adikire masiku awiri kapena atatu kuti ayambe kufesa fodya panazalepo, adafotokoza Jere. Iye adati mlimi ayenera kuthira feteleza wokwana makilogalamu atatu asadafese fodya uja. Akafesa fodyayo athire mankhwala kuti aphe tizilombo monga nyerere zomwe zikhoza kudya mbewuyo. Mankhwala ena ofunika kuthira panazale ndi amene amapha tizilombo toyambitsa matenda ena mufodya, adatero Jere. Malinga ndi Jere, mankhwalawa amafunika kusungunula mutheka la madzi a mukheni ndi kuwathira panazale paja pataikidwa kale maudzu. ",4 "Boma Lati Dongosolo La Zachuma Lithandza Anthu Kupeza Ngongole Wolemba: Sylvester Kasitomu w.radiomaria.mw/wp-content/uploads/2019/09/botomani.jpg"" alt="""" width=""294"" height=""333"" />Wati anthu apeza ngongole mosavuta-Botomani Boma lati dongosolo la zachuma la mchaka cha 2019 mpaka 2020 lithandiza kuti anthu adzitha kubwereka ndalama zoti adzitha kutukulira maanja awo kaamba koti boma laika ndalamazi mu dongosololi. Nduna ya zofalitsa nkhani a Mark Botomani anena izi pachilumba cha Chisi pa nyanja ya Chirwa mboma la Zomba, pamsonkhano othokoza anthu a pachilumbacho powavotera pa chisankho cha pa 21 May chaka chino. A Botomani omwenso ndi phungu wa kunyumba ya malamulo mdera la Zomba Chisi, ati ena mwa anthu omwe adzapindule ndi ngongoleyi ndi asodzi omwe amapha msomba pa chilumbacho. Pankhani za umoyo, iwo ati boma liyesetsa kumanga chipinda chochilira amai oyembekezera pachilumbacho ndipo powonjezera apo ati boma lachotsanso msonkho omwe anthu amaitanitsira magetsi a mphamvu ya dzuwa ndi cholinga choti anthu adzitha kugula magetsiwa. Mmawu ake Gulupu Village Headman Tchuka ya pa chilumbacho, yapempha anthu kuti asiye kumanga nyumba za udzu okhaokha mmadzi a mnyanja ya Chirwa pofuna kuchepetsa vuto lakuphwa kwa madzi pa nyanjayo. Anthu ambiri omwe akumanga mbowera zawo mmphepete mwa nyanjayi amagwiritsa ntchito udzu omwe amaumweta mphepete mwa nyanjayi choncho tipepha boma kuti libweretse anthu achitetezo ku nyanjayi kuti athamangite omwe akumanga zimbowera zawo mphepete mwa nyanjayi, anatero Group Tchuka. Mwazina iyo yapempha boma kuti lipereke achitetezo omwe adzithamangitsa asodzi omwe akumamanga mbowelazi mmadzimo. ",2 " Uve wanyanya mmisika Akugwiritsa madzi a mzithamphwi Tituluka mumsika munomabutchala Kafukufuku yemwe Tamvani wachita sabata ino waonetsa kuti uve wanyanya mmisika yambiri mdziko muno, maka ya mmakhonsolo a mizinda ya Blantyre ndi Lilongwe kaamba koti mulibe madzi a mmipope. Masamba ngati awa amafunika kutsukaasanagulitsidwe Chifukwa cha kusowa ukhondo mumsika waukulu mumzinda wa Blantyre, mabutchala aopseza kuti ngati khonsolo sichitapo kanthu atuluka mumsikawu chifukwa akhala zaka ziwiri tsopano popanda madzi aukhondo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Iwo akuti pakalipano akugwiritsa ntchito madzi amzithaphwi potsukira nyama ndi zipangizo zomwe amagwiritsa ntchito, pomwe ena akuti amachita kukagula madziwo kutali ndi malo a bizinesi yawo. Izi zikhoza kuika miyoyo ya ogula ndi ogulitsa nyama pachiopsezo chifukwa nyama yosasamalika bwino ikhoza kukhala gwero la majeremusi omwe athanso kuononga miyoyo ya anthu odya nyamayo. Koma mneneri wa khonsoloyi Anthony Kasunda wati khonsolo ya Blantyre sikudziwa kuti kumsikawu kudadulidwa madzi. Kasunda: Tsatirani malamulo Timakhala ndi anthu oyanganira misika ndipo amenewo amalumikizana ndi khonsolo pa nkhani za mabilu a madzi ndi magetsi ndi zina zonse. Nkhani mukunenayi ndi yachilendo kwa ife, adatero Kasunda. Loweruka sabata yatha, mabutchalawa adauza Tamvani kuti akhala akudandaulira khonsoloyi nthawi yaitali kuti ikonze zinthu koma palibe chomwe chikuchitika kupatula kulonjeza. Iwo adati mu 2014, khonsoloyi idakazula mamita a madzi ponena kuti mabilu akukwera kwambiri, koma akuti adasiya lonjezo loti nkhani yokhudza madzi aikonza. Butchala aliyense ali ndi chipinda chake chomwe amagulitsiramo nyama. Pomanga msikawu, chipinda chilichonse chidali ndi mpope wamadzi, koma mu 2014 khonsoloyi idadzazula mamita. Kuchokera apo mpaka lero tilibe madzi, adatero butchala wina. Panopa tikugwiritsa ntchito madzi amene amangodzitulukira pansi pafupi ndi msikawu, pena timakagula mzigubu. Iye adati poyamba akamalipira ndalama za lendi amaphatikizaponso za madzi malinga ndi bilu yomwe yatuluka ndipo khonsoloyi ndiyo inkakalipira ku Blantyre Water Board. Sitimvetsabe chifukwa chomwe adachotsera madziwa, chifukwa timalipira, koma tidadabwa akudzachotsa mamita Achikhala amadzachotsa ndi a Water Board bwezi mwina titadziwa chifukwa chake, adatero. Paganizo la mavendawa lotuluka kumsikawu, Kasunda adati malamulo oyendetsera mzinda wa Blantyre amaletsa kuchita malonda paliponse kotero ndi kuphwanya malamulo kutuluka mumsikawu. Aliyense wochita malonda mumzinda wa Blantyre akuyenera kutsatira malamulo onse ndipo palibe chifukwa choti wina aphwanye malamulowo mwadala, adatero. Kupatula nkhani ya madzi, mabutchala a mumsika wa Blantyre ati nkhani ina iwatulutse mumsikawu ndi anthu ena amene akugulitsa nyama mwachisawawa popanda zikalata. Kukumabwera galimoto zitanyamula nyama ndi masikelo awo. Akumagulitsa nyama paliponse pamene ife amatikaniza kutero. Chifukwa cha izi, nyama yathu sikuyenda malonda. Tadandaula koma sizikumveka. Anthuwa alibe zikalata zogulitsira nyama koma sakuletsedwa. Timadula chiphaso chophera nyama chomwe ndi K21 000, chipinda chogulitsira timalipira K17 000 pamwezi, koma ena akuwalola kumagulitsa nyama paliponse, adatero mmodzi wolankhulira mabutchalawo. Pankhaniyi, Kasunda adati khonsolo sidapereke chiphanso cha bizinesi kwa ogulitsa nyama paliponse ndipo anthu amene amakhazikitsa bata mumzinda wathu [ma rangers] amalanda malonda alionse amene akuchitikira malo osayenera. Nawo msika wa ku Limbe mumzindawu mavutowa aliponso chifukwa nakonso madzi adawadulira mu 2014. Podula madziwo, khonsoloyi idatsegula malo amodzi amene anthu onse mumsika akutungapo. Ku Lilongwe, misika ya Tsoka, Kawale, Biwi ndi Mchesi ukhondo ulipo kaamba koti madzi aukhondo aliko. Koma mumsika wa Lilongwe Central womwe ndi waukulu, uve akuti wafikapo pamene mavenda akugwiritsa ntchito madzi amumtsinje wa Lilongwe. Kondwani Juwawo, yemwe amagulitsa tomato mumsikawu, adati akafuna madzi abwino ndiye amakagula kwa munthu wina pafupi ndi msikawo. Madziwa ndi odula chifukwa ndi a munthu osati a Water Board. Ngati tilibe ndalama timakatunga kumtsinjeko kudzatsukira tomato ndi kuwaza ndiwo zamasamba kuti zisanyale, adatero Juwawo. Ku Mzuzu zinthu akuti zili bwinoko chifukwa misika ya Luwinga, Zigwagwa ndi msika waukulu wa Mzuzu mulibe mavuto a madzi. Lachitatu Tamvani itazungulira misikayi, yomwe imakhala ndi anthu ambiri, zinthu zidaoneka zosinthirako pamene wamalonda aliyense adali ndi mwayi wa madzi aukhondo mmisikayo. Mkulu woona za umoyo mumzinda wa Mzuzu, Felix Namakhuwa, adati misika yonse kumeneko ili ndi madzi monga njira imodzi yolimbikitsa nkhani za ukhondo. Timawalimbikitsa za kufunika kotsuka malonda awo komanso kusamba mmanja asadayambe kugulitsa malonda awo. Ichi nchifukwa chake venda aliyense ali ndi madzi mmisikayi, adatero Namakhuwa.Zowonjezera: Martha Chirambo ndi Steven Pembamoyo. ",2 " Nandolo mpatali Ubwino wa nandolo si uli pa kupeza ndalama zochuluka kokha komanso zina zambiri, watero mkulu woona za mbewu za mgulu la mtundu wa nyemba ku Bvumbwe Research Station, Richard Andasiki. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Andasiki adati pambali poti mbewuyi ndi imodzi mwa mbewu zimene alimi angaphe nazo makwacha ochuluka, ilinso ndi chakudya chabwino chomanga thupi, imabwezeretsa chonde mnthaka, siyivuta kulima, ndi yosavuta kusunga ngakhalenso kusamalira pamene ili mmunda. Iye adatinso mitengo ya nandolo ndi nkhuni zabwino. Nandolo amabwezeretsa chonde mnthaka munjira ziwiri. Poyamba masamba ake akayoyokera mmunda, amaola mosavuta ndipo amakhala manyowa amphamvu. Kachiwiri, mizu ya nandolo imakhala ndi tizinthu tooneka ngati totupa tomwe timakhala ndi tizilombo tobwezeretsa michere yotchedwa nitrogen mChingerezi yomwe ndi yofunika kwambiri ku mbewu, iye adatero. Nandolo ali ndi phindu lochuluka Andasiki adafotokoza kuti chifukwa cha kubwezeretsa chonde mnthakaku, mbewu zina monga chimanga zimapindula. Iye adati nandolo salira zipangizo zochuluka monga feteleza komanso safuna chisamaliro chochuluka nchifukwa chake amachita bwino ngakhale abzalidwe pamodzi ndi chimanga kotero safunanso chisamaliro chapadera chifukwa pamene mlimi akusamalira chimanga chake, amakhala akusamaliranso mbewuyi koma ngati wabzalidwa payekha, chachikulu ndi kupalira basi. Isaac Mpunga, mmodzi mwa alimi a nandolo a mboma la Nsanje adati mbewuyi ndi yomwe yachita bwino kwambiri kudera kwawoko ngakhale mvula inadukiza. Nandolo amafuna mvula nthawi yochepa nchifukwa chake amatha kukula komanso kubereka mvula italeka kotero ndi mbewu yothandiza, iye adatero. Ngakhale izi zili chomwechi, alimi a nandolo chaka chino adandaula kuti mbewuyi yayamba ndi mtengo otsika kwambiri kusiyana ndi chaka chatha. Jonath Goliath, mmodzi mwa alimi omwe amalima mbewuyi mochuluka ngati bizinesi yake, wa mboma la Neno wati izi ndizokhumudwitsa kwambiri chifukwa mtengowu sukupereka chiyembekezo chilichonse. Padakalipano, nandolo ali pa K100 pa kilogalamu chonsecho chaka chatha adayamba pamtengo wa K500 pa kilogalamu ndipo adachita kutsika nkufika pa K250 pa kilogalamu. Zikudabwitsa kuti akachoka pamenepa afika pati, adatero iye. Goliath adadabwa kuti ngakhale boma lidaika mtengo wotsikitsitsa wa nandolo kukhala K320 pakilogalamu, ogula akugula pa K100. Mitengo yopendereza alimife ogulawa akuitenga kuti? adadabwa iye. Mlimiyo adati zaka za mmbuyomu, mbewu ya nandolo ndi yomwe idali ndi phindu koma panopa siikulongosoka zomwe zikusowetsa alimi pothawira. Arthur Ngwende, woona za malonda kukampani ya Farmers Organisation Limited (FOL) imalimbikitsa alimi kugwiritsa ntchito mbewu zamakono komanso mankhwala othandiza kuti nandolo akule bwino ndiponso imatha kudziwa za momwe misika ya mbewuyi ikuyendera, wati alimi akhonza kudikirira kaye kufikira nandolo wawo atauma bwinobwino. Nandolo wangokololedwa kumene kotero amakhala wolemera kwambiri chifukwa amakhala akadali ndi madzi choncho zikhonza kutheka kuti ogulawa akuchitira dala kumagula pamtengo woterewu nchifukwa chake alimi sakuyenera kuthamangira, iye adatero. Ngwende adatinso dziko la India, limene limagula mbewuyi kwambiri mdziko lino, layamba kulima lokha, choncho silikugulanso nandolo wochuluka ngati kale. Andasiki adavomereza kuti alimi akuyeneradi kusunga kaye mbewuyi kuti ayambe aona momwe mitengo ikhalire miyezi ikubwerayi. Iye adati kuti asungike bwino komanso kwa nthawi yaitali, choyambirira amuumitse kufikira chinyontho chisapyole ndi 12 peresenti ndipo akatero amuthire mankhwala chifukwa kupanda kutero amafumbwa. ",4 " EU, WORLD BANK DISMISS ATUPELE Baum: I hope this clarifies it The European Union (EU) and the World Bank yesterday distanced development partners from remarks by United Democratic Front (UDF) presidential candidate Atupele Muluzi purporting that donors will only resume budget support if there will be regime change in the May 20 Tripartite Elections. Atupele, the youngest of the 12 presidential candidates, told a rally in Mzuzu on Sunday that alongside his running mate Godfrey Chapola they met representatives of the International Monetary Fund (IMF), the World Bank and other development partners last Friday. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi He claimed the development partners told opposition leaders they would only support the budget if there is change of government. Said Atupele: On Friday, Dr Godfrey Chapola and I met with World Bank, International Monetary Fund [IMF] and Malawis donor partners who told us openly that if we dont change government this year, then we will revert to zero-deficit budget. Today, the Government of Malawi has already started to put in place zero-deficit budget and you all know what this means, the problems we encountered will come back to haunt us if we continue with this government. They [donors] have told us openly that because of Cashgate, issues of theft and economic mismanagement, they will not inject any money if things dont change. But in a written response to a questionnaire from The Nation to verify Atupeles claims, EU head of delegation Alexander Baum said whereas he did not personally listen to Atupeles address, disbursement of budget support is based on macro-economic stability as assessed by the IMF and the public finance management-related assessments of fiduciary risks. Said Baum: [The Malawi] government has implemented a number of actions, but many actions necessary to fix the public finances are still work in progress. Each partner assesses its fiduciary risks and takes decisions on this basis. There are no political criteria linked to budget support in Malawi other than what we call the fundamental principles, i.e. human rights, democracy etc. There is consequently not a link to a specific government and I have doubts that any colleague from the international partners would have said something different. I hope this clarifies it. In an earlier interview, Zeria Banda, who is responsible for communications at the World Bank African Regional Office, said when the World Bank met with UDF members, nothing was said regarding elections. She said: We met with leaders of various political parties, including PP [Peoples Party], MCP [Malawi Congress Party] and UDF to share our perspectives on the state of the economy and how to sustain reforms for more meaningful economic development. We also discussed agricultural reforms. We did not touch elections or results thereof. Malawis national budget is financed 40 percent by donors on the recurrent expenditures and 80 percent on development expenditure. Last November, the countrys major donors under the Common Approach to Budget Support (Cabs), to which Baum is co-chairperson, announced the withholding of $150 million in budget support in protest over plunder of public resources at Capital Hill widely known as Cashgate. Last week, an IMF mission from Washington led by Tsidi Tsikata said the IMF will wait for the elections before it releases a $20 million (about K8.4 billion) disbursement into the government purse as part of the Extended Credit Facility programme. Tsikata also said the mission had proposed to return to Lilongwe in June to confirm the recommendations agreed before submitting a report to the IMF management and Executive Board. ",11 " Zavutanso ku Mozambique Othawa nkhondo ayamba kufika mdziko muno Zavutanso ku Mozambique. Nkhondo ya pachiweniweni pakati pa otsatira chipani cholamula cha Frelimo ndi chotsutsa cha Renamo yagundikanso ndipo nzika zina za mdzikomo zayamba kuthawa nkhondo kukhamukira mdziko muno pofuna kupulumutsa miyoyo yawo. Koma ngakhale izi zili choncho, mtendere sadaupezebe. Ambiri akugona kumimba kuli pepuu, alibe zovala, zofunda komanso pokhala. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Umu ndi momwe zilili mmudzi mwa Kapise kwa Senior Chief Nthache mboma la Mwanza komwe kwaunjikana nzika za dzikolo. DC wa bomali, Gift Rapozo, watsimikiza kuti zawathina masamalidwe a nzikazo chifukwa kuofesi kwawo kulibe chakudya komanso matenti oti asamalire anthuwa pamsasa pomwe afikirapo. Zikatere maso amakhalano kuboma kuti litithandize ndi chakudya komanso malo oti anthuwa akasungidwe. Ife ndiye tagwira njakata chifukwa tilibe chakudya, adatero Rapozo polankhula ndi Tamvani kumayambiriro a sabatayi. Othawa nkhondowa akuti adayamba kufika mdziko muno pa 5 July ndipo pofika Lolemba lapitali nkuti anthu 678 atafika mmudzi mwa Kapise. Mdziko la Mozambique mudabuka nkhondo ya pachiweniweni mchaka cha 1977 patangopita zaka ziwiri chithereni nkhondo yomenyera ufulu wa dzikolo mchaka cha 1975. Nkhondo ya pachiweniweniyo idatha mu 1992 ndipo chisankho choyamba cha matipate chidachitika mu 1994. Chipani cha Frelimo ndicho chidapambana. Malinga ndi kafukufku wathu pa Intaneti, mmene nkhondoyo imatha nkuti anthu 1 miliyoni atataya miyoyo yawo pophedwa ndi asirikali a boma komanso zigawenga za Renamo, kunyentchera ndi matenda ena osiyanasiya monga malungo, kamwazi, likodzo ndi khate. Ena 500 000 adalibe pokhala komanso anthu 5 miliyoni adali atathawira maiko ena kuti akapeze mpumulo. Dziko la Malawi ndilo linkasunga othawa nkhondo a ku Mozambique oposa maiko ena onse oyandikana nawoanthu osachepera 1 miliyoni adasungidwa kumisasa mmaboma a Nsanje, Chikwawa, Mwanza ndi maboma ena. Ku Nsanje kokha kudali nzika za ku Mozambique 200 000, kuposa chiwerengero cha eni nthaka mbomalo. Ngakhale dziko la Malawi lidali pamavuto aakulu a zachuma ndi kuonngeka kwa chilengedwe kaamba kosunga othawa kwawowa, lidachitabe chamuna kuonetsa umunthu powapatsa zithandizo zosiyanasiyana kuti ayiwale kwawo, zomwe zidasangalatsa bungwe la United Nations ndinso maiko ena akunja. Chodabwitsa nchoti pankhondo ya pachiweniweniyo, boma la Malawi, pansi pa ulamuliro wa pulezidenti wakale, malemu Dr Hastings Kamuzu Banda, linkathandizira mbali zonse za Frelimo ndi Renamo. Posafuna kuonetsa kukondera, mwamseri Kamuzu ankagwiritsa ntchito Apayoniya (Malawi Young Pioneers) kuthandizira Renamo pomwe ankatumiza asirikali ankhondo a Malawi Army kuthandizira Frelimo pofuna kuteteza katundu wa boma la Malawi amene ankadzera mdzikolo. Bata ndi mtendere zidayamba kukhazikika mdzikomo koma pofika mchaka cha 2013 ziwawa zidayambiranso ndipo mpaka lero mtendere weniweni ukusowekera moti kumenyana pakati pa otsatira zipani za Frelimo ndi Renamo kwabukanso. Anthu mdzikomo akhala akupempha mtsogoleri wawo, Filipe Nyusi, yemwe wangotha miyezi 6 chilowereni mboma, kuti achite machawi pokambirana ndi Afonso Dhlakama, mtsogoleri wa Renamo, pofuna kuthetsa kusagwirizanako. Msabatayi, Nyusi adauza nyumba zofalitsa nkhani mdzikomo kuti achita chotheka kukambirana ndi Dhlakama pofuna kukhazikitsa bata mdzikomo. Kusamvana kwa mbalizi kwachititsa kuti anthu wamba, maka amene akukhala ku Mkondezi, malo amene achita malire ndi dziko lino, akhale akapolo pamene akuwayatsira nyumba komanso kuphedwa, zomwe zachititsa kuti ena athawe mdzikomo ndi kukabisala mmaiko oyandikananawo monga Malawi. Komabe kusamala anthuwa kukuoneka kuti kukhala kovuta kudziko la Malawi lomwe kumayambiriro a chaka chino lidali ndi mavuto a kusefukira kwa madzi lomwe lidachititsa kuti anthu alephere kukolola chakudya chokwanira. Chipani cha Renamo chimakana kuti chidagonja mchisankho cha mu 2014 zomwe zachititsa kuti zipani ziwirizi zikhale pachimkulirano. Kaamba ka izi, Dhlakama wakhala akuopseza kuti ayambiranso kuchita mtopola womwe ubutse nkhondo mdzikomo pokhapokha dandaulo la chipani chake litamveka. Usiku wa Loweruka lathali, Dhlakama adauza nyumba ina youlutsira mawu mdzikomo kuti asirikali ankhondo okwana 53 aphedwa kale chiyambireni mwezi wa June. Kelvin Sentala wa bungwe la United Nations High Commissioner for Refugees (UNHCR) wati bungwe lawo likudziwa kuti anthuwa alowa mdziko muno, koma adakana kufotokoza zambiri ponena kuti mneneri wawo, Monique Ekoko, yemwe foni yake simayankhidwa, ndiye angalankhulepo. Nduna yoona za mdziko, Atupele Muluzi, sadayankhe foni yake kangapo konse Tamvani idayesera kumuimbira. ",11 "Mmodzi Wafa, Atatu Atsopano Apezeka ndi Coronavirus Nduna yowona zaumoyo mdziko muno, Jappie Mhango watsimikizira za imfa ya mayi wina yemwe wamwalira ndi nthenda ya COVID -19 mdziko muno. Mhango wanena izi pa msonkhano wa atolankhani omwe komiti yapadera yomwe ikuwona za matendawa inachititsa lero mu mzinda wa Lilongwe. Ndunayi yati mayiyu yemwe ndi wa zaka 51 amakhala mdziko muno koma inali mzika ya mdziko la India ndipo wafika mdziko muno posachedwapa kuchokera ku United Kingdom. Ndunayi yalengezanso kuti anthu atatu atsopano apezeka ndi nthendayi pomwe wati awiri ndi a mu mzinda wa Blantyre pamene mmodzi ndi wa mboma la Chikwawa. Malinga ndi a Mhango munthu mmodzi wamu mzinda wa Blantyre ndi mayi wa zaka 34 yemwe watenga matendawa kuchokera kwa mbale wake yemwe anapezeka ndi nthendayi pa 3 April chaka chino. Ndipo wina ndi mayi wa zaka 28 yemwe anafika mdziko muno pa 19 March kuchokera ku United Kingdom. Ndipo ndunayi yati munthu wachitatu ndi bambo wina wa zaka 30 wa mboma la Chikwawa yemwe anafika mdziko muno pa 16 March kuchokera mdziko la South Africa. Zimenezi zikutanthauza kuti anthu amene apezeka ndi nthendayi mdziko muno padakalipano akwana asanu ndi atatu (8). ",6 " Waganyu: Kulibe mipira yokonzekera zoona? Bungwe la FAM laletsa anyamata a Flames kuti asachite zokonzekera chifukwa ndalama palibe. Pofika dzulo zidali zisadadziwike ngati Malawi isewere ndi Mali komanso Ethiopia. Mndondomeko ya zachuma, Flames idalandira K70 miliyoni mmalo mwa K400 miliyoni. Pano ndalamayi yatha ndipo FAM palibe ingachite koma kulepheretsa zokonzekerazi. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Kodi apa tidzudzule boma kapena tiloze zala FAM? Vuto la mpira mdziko muno si lachilendo ndipo ife sitikudzidzimuka kumva kuti boma lili chabechabe. Misonkho yathu ikumakhala yokangobetsa osati kugwirira ntchito yomwe ifeyo tikufuna. Anthu akuzunzika kaamba kosowa mankhwala komanso zina. Apanso ndi izi kuti mpira tsopano ukupita pansi. Masewero a mpira wamiyendowu ndiwodula kwambiri kusiyana ndi ena. Ife tikuona kuti Amalawi sitidakonzeke kuti tizipezeka nawo mmipisano monga wa Afcon chifukwa mapeto ake tidzikhala ndi ndalama zosewerera gemu koma kulephera kupeza zokonzekera. Sitikudziwa kuti anduna athu adziti chiyani apapa polingalira kuti adalonjeza kuti Flames ilandira ndalama zake mpaka kumaliza mpikisanowu? Tikudabwa chifukwa tikayangana kuchipatala kuli mavuto, ku ulimi ndiye wosakamba, nako ku zamaphunziro ndi misewu ndiye mavuto a nkhaninkhani. Ndiye msonkho wathu uzigwira ntchito yanji? Kapena ntchito ya misonkho yathu nchiyani? Kapena mufuna izingobedwa pamene ife tikuvutika? Ifetu zatikwana ndipo chiyembekezo chathu nchakuti nduna ya zamasewero Grace Chiumia alankhulapo pa zomwe zikuchitikazi. ",16 " Apereka ambulansi ku Bangwe Katika: Yatha miyezi iwiri Kwa kanthawi anthu makamaka amayi oyembekezera akhala akuvutika mayendedwe popita ku chipatala cha Bangwe Clinic mumzinda wa Blantyre. Anthu omwe amavutikawa ndi omwe akukhala ku Mpingwe ndi Mvula chifukwa kumaloko sikufika ma minibasi kaamba koipa kwa msewu. Pano mavutowa tsono angakhale mbiri yakale pomwe anthuwa alandira minibasi komanso ambulance yomwe idziyenda kumeneko. Zinthuzi zaperekedwa ndi yemwe amakonza masewero a nkhonya komanso amiyendo Justice Katika. ",6 " Agwidwa ukapolo ku Ntchisi Madzi achita katondo kwa T/A Malenga mboma la Ntchisi komwe Gulupu Malenga, Peku Wakuda ndi Munkana aletsa anthu a mmudzi mwa Peku Woyera kukhala nawo pa zochitika zilizonse mderali kuphatikizapo maliro, ukwati komanso kupita kumsika wawo waukulu potsatira mkangano wa malo. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Nkhaniyi ikuti mfumu yaingono Peku Woyera idawina mlandu wa malo womwe udaweruzidwa ndi magulupu atatuwa. Malinga ndi Peku Woyera, magulupuwa ataona kuti zake zayera pamlanduwu, adanenetsa kuti amkhaulitsa. Akuti asayende: Peku Woyera Chilango chake anthuwa adagwirizana kuti ine ndi anthu a mmudzi mwanga tisiye kukhala nawo pazochitika mpaka kutiletsa kupita kukagula zinthu kumsika wathu waukulu ati kaamba koti ndidawina mlanduwo, idatero mfumuyo, yomwe dzina lake la pamsonkho ndi Tisiyenji Daniyele. Mfumuyo idati anthuwa adaletsedwanso kukhala nawo pamisonkhano ya chitukuko. Ngakhale ana awaletsa kutenga nawo mbali pazamasewero, pomwe amayi awathamangitsa kumabanki a mmudzi ndi makalabu a ulimi. Moti ndikulankhula pano mayi wina adamulanda katundu wosiyanasiyana pakhomo yemwe adagula patauni yathu yaingono, Peku Woyera adatero. Iye adati pano anthuwa akudalira msika waukulu wa Ngombe womwe uli pamtunda wa pafupifupi makilomita asanu. Peku Woyera adati ngakhale nkhaniyi idatengeredwa kubwalo la milandu komwe adalamulidwa kuti azisonkhana nawo ndi anzawo, magulupuwo akanitsitsa kuchotsa chiletsocho. Ndife akapolo mmudzi mwathu momwe, adatero Peku Woyera. Polankhulapo, gulupu Malenga adavomereza za nkhaniyi ndipo adati chidatsitsa dzaye kuti magulupu atatuwo apereke chiletso chokhwimachi ndi mwano womwe Peku Woyera adachita ponyozera zisamani zomwe amalandira. Malenga adati mwachikhalidwe chawo, zilango monga izi zimaperekedwa kwa anthu amwano ndi cholinga choti aphunzire mwambo. Iye adati mudzi wonse walandira chilangochi chifukwa udakhudzidwa pamkangano wa malowo. Ife tikufuna kuti mfumuyi ndi anthu ake azibwera kubwalo akalandira chisamani, koma akapitiriza mwano sitingachitire mwina koma kuwalanga powasala, Malenga adatero. Koma Clement Zindondo, mmodzi wa akuluakulu a bungwe lomwe si laboma lomwe likutengapo gawo pa achinyamata ndi chitukuko la Ntchisi Organisation for Youth and Development (NOYD), adati anthuwa akusowekera thandizo kaamba koti magulupawa awaphwanyira ufulu wawo wosonkhana ndi anzawo. Ife tikudabwa kuti bwanji magulupuwa sakulemekeza chigamulo cha bwalo la milandu? Apatu sakusamala za malamulo oyendetsera dziko lino ndipo ndikhulupirira kuti akhoti achitapo kanthu nkaniyi ikawapezanso, Zindondo adatero. ",7 "Mipingo Ipewe Tsankho-Papa Wolemba: Thokozani Chapola Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse papa Francisco lachinayi wapempha mipingo kuti idzikhala patsogolo kuperekeza anthu kwa Mulungu posatengera kusiyana kwa mitundu kapena kochokera. Papa Francisko Papa walankhula izi pa imodzi mwa miyambo ikulu ikulu yomwe anali nayo ku likulu la mpingowu ku Vatican. Iye wati mpingo usamakhale ndi malire kapena tsankho pakati pa akhristu ake pomwe ukufuna kupereka masacrament kapenanso kulandira anthu mu mpingowo. Mtsogoleri wa mpingo wakatolikayu wati monga khomo la kumwamba limakhala lotsekula nthawi zonse, mipingo kudzera mwa atsogoleri awo, akuyenera nawonso kumasula milandu ya akhristu omwe anamangidwa. Pamenepa PAPA FRANCISCO anapereka chitsanzo cha akhristu oyamba omwe anati anali kuyendera limodzi ndipo sanali kusungirana mangawa. ",14 " PAC iunguza za boma la chifedulo Nthumwi zomwe zimakumana mumzinda wa Blantyre kukambirana za nkhani yakuti zigawo za dziko lino zizikhala ndi mtsogoleri wakewake pansi pa mtsogoleri wa dziko zati nkhaniyi kuti iyende bwino mpofunika kusintha malamulo ena. Mfundoyi ikugwirizana ndi zomwe adanena mphunzitsi wa za ndale kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, Blessings Chinsinga, kuti popanda kuunika malamulo, nkhaniyi ikhoza kudzetsa chisokonezo. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Choyamba tiunike kuti malamulo athu akutinji chifukwa mukhoza kukhala ndi zigawo zodziyimira pazokha zomwe zingamakolanenso chifukwa cha malamulo omwe mukutsata, adatero Chinsinga. Msonkhanowo udakonzedwa ndi bungwe la mipingo la Public Affairs Committee (PAC) ndipo cholinga chake chidali kuunika chomwe chidayambitsa nkhaniyi ndi kukambirana momwe ingayendere. Malinga ndi wapampando wa bungwe la PAC, Mbusa Felix Chingota, nthumwi za kumsonkhanowo zidapeza kuti nkhaniyo idachokera pakusamvetsetsana pa momwe zinthu zina zikuyendera. Nthumwi zidapeza kuti nkhani monga kusankhana kochokera, kukondera pakasankhidwe ka maudindo, kusiyanitsa pakagawidwe ka zinthu ndi kupondereza zitukuko zomwe atsogoleri ena adayamba ndi zina mwa zinthu zomwe anthu akuona kuti ndi bwino aziyendetsa okha zinthu, adatero Chingota. Mlangizi wa mtsogoleri wa dziko lino pankhani za mgwirizano wa mdziko muno, Vuwa Kaunda, adati ndi cholinga cha mtsogoleri wa dziko lino, Peter Mutharika, kuti anthu azipereka maganizo awo kuti zinthu ziziyenda bwino. Kaunda adati Mutharika adalumbira kuti adzalemekeza malamulo a dziko lino omwe amapereka mwayi kwa Amalawi wolankhula zakukhosi kwawo. Mafumu nawo ayamikira zomwe lidachita bungwe la PAC pokonza msonkhanowo ndi zomwe nthumwi zidagwirizanazo. Paramount Chief Chikulamayembe wa ku Rumphi adati nzopatsa chidwi kuti boma ndi mabungwe akugwirizana pankhani yofuna kudzetsa umodzi ndi mtendere pomanga mfundo zoyendetsera nkhani zikuluzikulu monga imeneyi. Apa ndiye kuti zinthu ziyenda kusiyana nkuti anthu azingopanga phokoso lopanda tsogolo lake. Tionera kwa akuluakuluwo kuti akonza zotani, adatero Chikulamayembe. Koma malinga ndi Chinsinga, nkhaniyi ingaphweke Amalawi atalangizidwa bwino momwe ulamuliro wotere ungayendere. Iye adati nzomvetsa chisoni ndi kuchititsa mantha kuti Amalawi ena akungotsatira maganizo a anzawo chifukwa chosamvetsetsa. Iyitu si nkhani yaingono koma pakuoneka kuti anthu ambiri sakumvetsetsa mutuwu mmalo mwake angotsatirapo poti walankhulayo amamukhulupirira. Mpofunikanso kumasulira bwinobwino tanthauzo la nkhaniyi nkuphunzitsa Amalawi kuti azipereka maganizo awo enieni, adatero Chinsinga. Iye adati ulamuliro wotere ndi njira yoyendetsera boma yomwe dziko limagawidwa mmagawo omwe amayendetsa okha ntchito za chitukuko koma ali pansi pa ulamuliro wa mtsogoleri mmodzi. Iye adati kutengera pamgongo nkhani yotereyi kukhoza kubweretsa kusamvana ndi chisokonezo pazinthu zingonongono. Muganizire apa. Dzikoli ndi lalingono kwambiri komanso njira zobweretsa ndalama nzochepa. Pofuna kugawa, mpofunika kuunika bwinobwino mmene malire akhalire komanso kuti chigawo chanji chitenga chiyani, adatero Chinsinga. Mkulu wa bungwe la PAC, Robert Phiri, adati msonkhano womwe bungweli lidakonza udakambirana zina mwa nkhani zoterezi. Msonkhanowo udachitika Lolemba ndi Lachiwiri mumzinda wa Blantyre ndipo udabweretsa pamodzi akuluakulu a mnthambi za boma, mabungwe oyima paokha ndi otsata mbiri ya dziko lino. Phiri adati zomwe adakambirana akuluakuluwo azitulutsa ndi kuzipereka kuboma ndi mabungwe kuti zipereke chithunzithunzi cha mmene angagwirire ntchito ndi anthu pankhaniyi. Mmbuyomu, kafukufuku yemwe nyuzipepala ya The Nation idachita adasonyeza kuti aphungu 61 mwa 100 alionse adati nkhaniyi itapita ku Nyumba ya Malamulo akhoza kuikana. Nyuzipepalayi itafunsa aphungu 122 mwa 193, 75 adati angakane mfundoyi, aphungu 17 adali asanaganize ngati angaivomereze kapena ayi pomwe aphungu 30 adati angavomereze za mfundoyi. Mchaka cha 2006, mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika adanena kuti boma la mtunduwu likhoza kuthandiza pachitukuko cha dziko lino. Uku kudali msonkhano wounikira malamulo a dziko lino. Koma masiku ano, Mutharika amatsutsana ndi maganizowa ati kugawa dziko. Pamsonkhanowo padali a zipani zosiyanasiyana, mafumu, azipembedzo, mabungwe omwe si aboma ndipo amayendetsa zokambiranazo ndi sipikala wakale wa Nyumba ya Malamulo Henry Chimunthu Banda ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wakale wa dziko lino Justin Malewezi. ",11 " Kuthimathima kwa magetsi kwakhudzanso akumidzi Ndi Lolemba mmbandakucha wa pa 12 September, nthawi yangokwana kumene 4 koloko koma magetsi azima kale mboma la Mulanje. Chiyembekezo nchoti posakhalitsa ayaka. Gulu la alimi lopanga tsabola wa Zikometso Hot Chilli Sauce, maso akudikira kuti mwina magetsi ayaka nthawi iliyonse. Poyembekezera, asakaniza kale tsabola kuti magetsi akangoyaka ayambe kuphika mmakina awo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Akadadziwa akadaphika therere! Magetsi sadayake tsiku lonse. Pofika 7 koloko mmawa wa Lachiwiri, magetsi kuli chuu, zomwe zapangitsa kuti akataye zosakanizazo. Umu ndi momwe zikukhalia kwa anthu akumudzi amene sangakwanitse kupeza injini ya magetsi (generator). Makampani a alimi akulephera kuyendetsa malonda awo, zinthu zasokonekera chifukwa cha kuthimathima kwa magetsi, komwe kukulowa mwezi wachiwiri tsopano mdziko muno. Nalo bungwe lopanga ndi kugulitsa magetsi la Escom laneneratu kuti mavutowa anyanyira miyezi ikubwerayi chifukwa cha kuchepa kwa madzi omwe amapukusa makina opangira magetsi ku Nkula ndi ku Tedzani mumtsinje wa Shire. Monga akufotokozera wachiwiri kwa mkulu wa Zikometso, Amos Ambali, pasabata amapanga mabotolo a tsabola 2 100, koma pano akupanga osaposera 500. Timagwira ntchito Lolemba mpaka Lachisanu, koma masiku onsewa kukukhala kopanda magetsi. Mapeto ake tayamba kugwira usiku wokhawokha komanso Loweruka masana pamene magetsi akumayaka. Sizikupanganika, pena kukukhala kopanda magetsi tsiku lathunthu, zomwe zasokoneza bizinesi yathu. Kangapo konse tataya tsabola patatha masiku awiri popanda magetsi kupangitsa kuti tsabola wathu aonongeke, adatero Ambali. Nawo a Talimbika Agro-Processing and Marketing Cooperative Society, amene amapanga mafuta ophikira a Sunpower mboma la Salima, akuti magetsi akazima, amagulula makina awo ndi kuchotsa mpendadzuwa yense. Fanny Jodani ndi mmodzi mwa akuluakulu pa Talimbika ndipo akuti patha miyezi iwiri magetsi akuzimazima ndipo tsiku lililonse akumazima isadakwane 4 koloko nkumayaka 6 madzulo. Apapa tayamba kugwira ntchito usiku, komabe zikuvuta chifukwa pena kukumakhala kopanda magetsi. Magetsi akazima sitigwira ntchito ndipo timagulula makina athu, kuchotsa mpendadzuwawo, adatero. Talimbika imapanga malita 500 patsiku ngati magetsi akuyaka, koma pano tsiku likutha osapanga mafuta. Ali ndi antchito oposa 11 amene akufunika malipiro, kodi akumawalipira bwanji? Mkulu wa Talimbika, Pharison Chiwoko, akuti ili ndi vuto lalikulu. Magetsi akamayaka bwino, timapanga ndalama yoposa K3 miliyoni pamwezi. Mwezi unowo ngakhale K1 miliyoni sikwana. Timaononga K700 000 kuti tilipire antchito. Mutha kuona kuti mwezi uno ngati anthu alandire ndi mwayi, akutero Chiwoko. Nako ku Dowa zinthu sizili bwino. Watson Kamchiliko mkulu wa Madisi Agro-Processors Cooperatives, omwenso amapanga mafuta ophikira, wati pali mantha kuti angachotse antchito ena ngati sizisintha. Timapanga malita 2 000 patsiku. Lero zasintha, tikumapanga malita 2 000 pasabata, bizinesi yasokonekera. Tili ndi ogwira ntchito amene akulandira K150 000, kodi awa tingawalipirenso? adatero Kamchiliko. Nako kuchigayo kwasokonekera. Kamchiliko akuti anthu akugona kuchigayo kudikira kuti magetsi ayake pa boma la Dowa. Pena amayaka cha mma 10 koloko usiku, anthu amagona kuchigayo kuti akayaka agaitse, adatero. Kwa T/A Phambala mboma la Ntcheu, eni zigayo za dizilo apezerapo mwayi ndi kuzimazima kwa magetsi pamene akweza mtengo kuchoka pa K300 thini kufika pa K350. Koma uthenga kuchokera kubungwe la Escom sukupereka chiyembekezo kwa anthuwa. Mkulu wa bungweli, John Kandulu, akuti izi zikhala zikuchitika kuyambira mwezi uno mpaka December pamene mvula idzakhale itayamba. Kandulu akuti izi zili chonchi chifukwa mlingo wa madzi a mumtsinje wa Shire ndi wotsika ndipo kutsikaku kupitirira pokhapokha mvula itayamba. Chifukwa cha izi, tingokwanitsa kutapa 135 megawatts mmalo mwa 361 megawatts zomwe zichititse kuti magetsi akhale akuzimazima, adatero Kandulu. ",2 "Akhristu Awapempha Akonde Kuthandiza Radio Maria Malawi Wolemba: Glory Kondowe Akhristu a mpingo wa katolika mdziko muno awapempha kuti azithandiza Radio Maria Malawi. A Maxwell Chikafa omwe ndi mbusa wa dera la Mzimu Woyera 1 ku St. Marys Nzama Parish mu Diocese ya Dedza ndiwo alakhula izi, lamulugu lapitali pambuyo pa mwambo wa Thandizani Radio Maria omwe unachitikira ku tchalitchi cha Mzimu Woyera 1 Tsangano Turn Off komwe akhristu anathandiza wayilesiyi ndi ndalama yokwana Mk133, 860. Abusa Chikafa ati ngati anthu akonda kuthandiza Radio Maria, wayilesiyi singamakumane ndi mabvuto azachuma, ngati mmene ziliri zithu padakalipano, polingaliranso kuti wailesiyi yatha zaka 20 ikutumikira anthu pofalitsa nthenga wabwino. Wayilesiyi imatithandiza munjira zosiyanasiyana moti kufalitsa mnthenga wabwino wa Yesu khristu zomwe zimatipatsa chiyembekeza. Wailesiyi imasowa zinthu zosiyanasiyana ndiye tiyenera kuyithandiza pa nkhani ya zachuma. A Chikafa anatinso akhristu ena ayenera kuchita chotheka poyikapo chidwi kugwira ntchito ndi wailesiyi ndipo aliyese amene atenga nawo mbari pothandiza radio maria zingati kutenga nawo mbali kufalitsa uthenga wabwino pa zaka 20 zomwe wailesiyi yakhala ikufalitsa nthenga wabwino monga chitsulo chimodzi sichiwunda chulu. Iwo anathokodzaso anthu onse amene amagwira ntchito yozipereka ngati awulutsi komanso atolankhani awailesiyi ndi kuwapempha kuti apitilize ntchito yopambanayi. ",13 " Mtima pansiAPM Ngati aMalawi adali ndi chiyembekezo choti aona kusintha kwakukulu pachuma ndi zina ndi zina zokhudza moyo wawo pambuyo pa kulumbiritsidwa kwa boma latsopano lotsogozedwa ndi Pulezidenti Peter Arthur Mutharika ndi chipani chake cha DPP, asathamange magazi chifukwa izi sizitheka lero ndi lero. Izi zili choncho chifukwa mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika Lachiwiri adati aphungu a Nyumba ya Malamulo sakambirana ndondomeko ya chuma cha dziko lino (Bajeti) yomwe imayenera kuyamba pa 1 July, 2014 mpakana pa 31 June 2015. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Polankhula koyamba ngati mtsogoleri wa dziko lino mNyumbayo, Mutharika adati mmalo mwake ndondomekoyi adzaikambirana mwezi wa August pofuna kupereka mpata woti boma liunike bwinobwino kunthambi zosiyanasiyana zinthu zofunika mundondomekoyi. Iye adati mmalo mwake aphungu angokambirana za ndondomeko ya chuma chapadera chomwe boma ligwiritse ntchito kuyambira mwezi wa July mpakana September, 2014. Gawo 178 la malamulo oyendetsera dziko lino limalola kukhala ndi ndondomeko yongoyembekezerayi. Tinali ndi nthawi yochepa yokonza ndondomeko ya chaka chonse. Komanso tiyenera kuunikira bwino ndalama zomwe zatsala kuthunba la boma tisanakonze ndondomekoyi, adatero Mutharika. Nduna ya zachuma Goodall Gondwe akuyembekezeka kukapereka ndondomeko yoyembekezerayi sabata ya mawa. Tikapereka ndondomekoyi tikhala tikufunsa anthu zimene akufuna kuti tiganizire mundondomeko ya chuma ya chaka chonse, adatero Gondwe. Mwa zina, Amalawi ambiri chidwo chawo chagona poti boma la Mutharika litsitsa liti mitengo ya malata ndi simenti kuti osauka amene akugona nyumba zofoleredwa ndi udzu komanso zozira ndi donthi nawo athe kumanga zofolera ndi malata komanso zasimenti pansi. Pokopa anthu kuti adzachivotere chipanichi panthawi ya kampeni zisankho zisadachitike pa May 20, 2014, akuluakulu adalonjedza Amalawi kuti chipani cha DPP chikadzakhalanso mboma chimodzi mwa zinthu zoyambirira pofuna kutukula miyoyo ya Amalawi ku kutsitsa mitengo ya malata ndi simenti kuti aliyense azigona mnyumba yoyenerera. Akatswiri mnthambi zosiyanasiyana mdziko muno ati boma lingachite bwino pachitukuko cha dziko litatsata bwino mfundo zomwe Mutharika adanena potsegulira Nyumbayo. Akatswiriwa ati Mutharika adanena mfundo zabwino zokhudza chitukuko koma sadatambasule bwino momwe mfundozo bioma lidzakwaniritsire. Zina mwa mfundo zomwe akatswiriwa ayamikira ndi zotukula ntchito za umoyo, ulimi ndi maphunziro koma ati sizikutambasula bwino mmene zidzayendere. Dalitso Kubalasa, mmodzi mwa akatsiwiriwa, yemwe ndi mkulu wa bungwe la Malawi Economic Justice Network lomwe ntchito yake ndi kuona mmene boma likuyendetsera chuma kuti chipindulire aliyense, wati boma lakhazikitsa mfundo zabwino kwambiri koma lalephera kufotokozera Amalawi mmene zidzayendetsedwere. Mfundozi ndizabwino kwambiri pachitukuko cha dziko lino ndipo nzosangalatsa kuti mtsogoleri akudziwa za mavuto omwe alipo pachuma. Koma ngakhale zili choncho, pali mfundo zina zofunika kuwongoledwa bwino kuti zigwire bwino ntchito yake, adatero Kubalasa pocheza ndi Tamvani Lachiwiri lapitali. Pankhani za umoyo, Mutharika adati, mwa zina, boma lidzakhazikitsa chisamaliro chapadera cha anthu ogwira ntchito mboma komanso lidzatukula miyoyo ya anthu ogwira ntchito mboma pakakwenzedwe pantchto ndi malipiro. Mkulu wa bungwe loona kuti ntchito za umoyo zikufikira anthu onse mofanana la Malawi Health Equity Network (Mhen), Martha Kwataine, akuti boma laganiza bwino pokhazikitsa chisamaliro chapadera cha anthu ogwira ntchito mboma, koma wadzudzula kuti silidatambasule bwino makamaka pa nthawi yomwe ntchitoyi idzayambe. Izi ndi zomwe takhala tikumenyerera kwa nthawi yaitali ndipo apa boma laganiza bwino kwambiri makamaka pakulonjeza kutukula miyoyo ya anthu ogwira ntchito za chipatala. Koma chomwe ndingapemphe boma ndi kutambasula bwinobwino nthawi yomwe izi zidzayambe kusiyana ndi kuti anthu azingokhala mumdima, adatero Kwataine. Mutharika adatinso boma lidzalimbikitsa ntchito zotukula achinyamata pokhazikitsa malo ophunzitsa achinyamata ntchito zosiyanasiyana kuti azikhala odzidalira paokha. Nduna yakale ya zachuma, Mathews Chikaonda, adati boma likuyeneranso kubwera poyera mmene ntchito yotukula achinyamatayi idzakhalire. Iye adati achinyamata ndi ofunika kwambiri pachitukuko cha mdziko choncho nkofunika kuika patsogolo ntchito zowatukula. ",11 "Anayi Anjatidwa Kamba Kochitira Chiwembu Mzika yaku Pakistan Apolisi ku Lilongwe amanga anthu anai omwe akuwaganizira kuti abera mzika in ya mdziko la Pakistan pachiwembu chomwe anayichitira. Watsimikiza za nkhaniyi-Benjamin Wachiwiri kwa mneneri wa apolisi mboma la Lilongwe Sergeant Foster Benjamin wati amunawo, Farouk Rahim, Lenias Wright, George Kasabola ndi Sautso Mandala awamanga lachinayi powaganizira kuti anaba ndalama zokwana 400 sauzande kwacha komanso lamya zammanja za ndalama pafupifupi 470 sauzande kwacha usiku wa pa 27 April chka chino. Sergeant Benjamin wati pakadali pano anthuwa awuvomela mlanduwu, ndipo apolisi akupitiriza kufufuza anthu ena omwe anali limodzi ndi akubawa omwe sanapezeke. Farouk Rahim wa zaka 33 ndi wa mmudzi mwa Mazengela mdera la mfumu yaikulu Malengachanzi mboma la Nkhotakota, Lenias Wright wa zaka 30, ndi wa mmudzi mwa Michenga mdera la mfumu yaikulu Mabuka ku Mulanje, George Kasabola wa zaka 30 ndi wa mmudzi mwa Moyo mfumu yaikulu Phambala komanso Sautso Mandala wa zaka 40 zakubadwa, ndi wa mmudzi mwa Chikadya kwa mfumu yaikulu Ganya mboma la Ntcheu. ",7 " Kwacha yagwa, valani zilimbe Anthu akumudzi ati boma lifulumire kuika njira zowatchinjirizira ku zomwe zingadze kaamba ka kugwa kwa ndalama ya kwacha. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Anthuwa ati ngakhale boma komanso akatswiri ena pachuma akulosera kuti kugwa kwa kwacha sikukweza mitengo ya zinthu moliritsa, izi zikhoza kukhala khambakamwa chabe. Anthuwa akuti katundu wina anayamba kale kukwera mtengo udyo banki yaikulu ya Reserve itangolengeza Lolemba kuti ndalama ya kwacha yagwa ndi pafupifupi theka la mphamvu yake. Tsopano pafunika K250 kuti munthu apeze $1 [Dollar] ya dziko la America, kuchoka pa K168. Kusinthaku kwadza ndalamayi itagwanso mu Ogasiti chaka chatha. Mlimi wa mzimbe, chimanga ndi mtedza wa mmudzi mwa Manjeza kwa T/A Kadewere mboma la Chiradzulu, Maginesi Banda wati kumeneko zinthu zinakwera Lolemba atangolengeza kuti Kwacha yagwa. Banda wati sopo wopaka yemwe adali K50 pano wafika pa K75 ndipo Shuga wachoka pa K230 kukagwa pa K300. Iye wati zina zomwe zakwera mtengo ndi mchere, nyemba komanso nsomba. Zinthu zakwera mtengo Mlimi yemwenso amachita bizinesi ya chimanga mmudzi mwa Mkombanyama kwa T/A Mwaulambia ku Chitipa wati kumeneko zinthu sizili bwino ndipo anthu akuvutika. Mkuluyo, Charles Kabaghe, wati malata a 32 geji aatali milingo 10 akugulitsidwa K5 900 kuchoka pa K2 800, pomwe thumba la fetereza wa 50kg la mtundu wa 23:21:0+4s tsopnao lafika pa K14 800 kuchoka pa K8 500. Kabaghe wati nkhuku zanyama zikugulitsidwa pa K1 500 kuchoka pa K700, pomwe dzira lili pa K80 kuchoka pa K30. Boma litithandize, watero Kabaghe. Katakwe wa phunziro la zachuma kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, Ben Kaluwa, wati ngati mabungwe ndi maiko akunja atapereka thandizo kudziko lino, ululu wa kugwa kwa kwacha sungakhale woriritsa kwambiri. Kaluwa wati thandizo la maiko ndi mabungwe lingaombole akumudzi ndi ena osowa kudzera mu zingapo monga malipiro a ntchito za chitukuko cha mmidzi. Ntchitoyi ndi monga yolambula misewu yomwe ogwira amalandirako kangachepe. Kumayambiriro kuno zinthu zikhala zovutirako koma posakhalitsapa titha kusimba lokoma chifukwa chokonza ubale ndi maiko komanso mabungwe othandiza dziko lino pachuma. Anthu angolimbikira kulima mbewu zoti angathe kugulitsa kumaiko ena monga fodya, thonje komanso nyemba chifukwa tsopano katundu wathu akhala wogulika, adatero Kaluwa. Akumudzi atetezedwe Koma Gulupu Chisinkha ya mboma la Mulanje kwa T/A Mabuka yati anthu ali ndi mantha kuti zinthu zivuta. Iyo yapempha boma kuti lionetsetse kuti anthu akumudzi atetezedwe. Anthu sangamvetse zomwe akuluakulu ena komanso boma likutanthauza akamati zinthu sizikwera. Chofunika nkuti aonetsetse kuti zomwe akulankhula zichitike chifukwa aliyense kumudzi kuno ali ndi mantha, adatero Chisinkha. Koma Kaluwa msabatayi ananenapo kuti mitengo ya zinthu sikuyenera kukwera moboola mthumba chifukwa amalonda ena anakweza kale mitengoyo. Iye anati pomwe mabanki samapezeka ndi ndalama zakunja, amalonda amakapeza ndalama ya dollar pamtengo wokwera mmisika yosavomerezeka ndi boma. Kunja kwa mabanki ovomerezeka, anthu mmisika yosavomerezeka ndi bomayo amasintha $1 pa mtengo wokwera, mpaka ena kumafika pa K300. Izi akatswiri adati zidali zizindikiro zoti ndalama ya kwacha inali itagwa kale pa chilungamo chake koma kuti boma limangochita liuma kuvomera izi. IMF ikutinji Sabata yatha, mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda, adauza atolankhani kuti alola ndalama ya kwacha ichepetsedwe mphamvu ngati bungwe loyanganira zachuma padziko lapansi la International Monitory Fund (IMF) ndi banki yaikulu padziko lapansi ya World Bank angatsimikizire dziko lino za thandizo la chuma. Msabatayi, potsatira kulola kuti kwacha itsike mphamvu, abwenzi a dziko lino pachuma monga IMF analengeza kuti akukonza ndondomeko zothandizira dziko lino kuti osaukitsitsa asamve ululu wakusintha kwa zachumaku. Iwo anati izi zikutsatira kusintha kwa kayendetsedwe kachuma komwe boma la Banda labweretsa molingana ndi ndondomeko za IMF komanso banki yaikulu padziko lapansi. Dziko lino limadalira ulimi komanso ndi limodzi mwa angapo mu Africa odikira thandizo la maiko ndi mabungwe akunja pa kapezedwe ka ndalama zakunja. Mwachitsanzo, mwa K100 iliyonse yomwe dziko lino limapata kuchokera ku malonda wogulitsa kunja, K60 imachokera ku malonda a fodya. Mwa K100 iliyonse ya ntchito za pansi pa ndondomeko ya chitukuko, K40 imachokera ku thandizo la maiko ndi mabungwe akunja. Koma kuchokera pomwe mitengo ku misika ya fodya inalowa pansi komanso kusokonekera kwa ubale ndi maiko akunja, dziko lino lakhala pa mpanipani wa zachuma. Ndalama zakunja Mmwezi wa Juni chaka chatha, mkulu wa IMF ku Malawi, Ruby Randall, anati kafukufuku mmayiko a kumwera kwa chipululu cha Sahara adasonyezapo kuti Malawi adali limodzi mwa maiko atatu omwe mapezedwe awo a ndalama zakunja adali wotsikitsitsa. Bungwe la IMF lakhala likupempha dziko lino kuti litsitse mphamvu ya ndalama ya kwacha koma mtsogoleri wakale wa dziko lino, malemu Bingu wa Mutharika, adakhala akumenyetsa nkhwangwa pamwala, ati kutero kungakweze zinthu mtengo moliza Amalawi. Kukanaku kunali chimodzi mwa zomwe Mutharika ananyanyula nazo maiko ndi mabungwe akunja mpaka kufika podula thandizo lawo. Apa Mutharika adaika ndondomeko ya chuma ya dziko lino yosadalira maiko ndi mabungwe akunja. Ngakhale mabungwe ena a mdziko muno nawo amati kunali koyenera kuvomera kutsitsa mphamvu ya kwacha, Mutharika anati sizitheka. Iye anati maiko ndi mabungwe akunja amapanikiza Malawi pa zachuma ncholinga chogwiritsa ntchito mavuti otsatira izi kuti afoole Malawi ndipo dzikoli lilole makhalidwe onyasa ponyengelera thandizo la ndalama. Iye anatchulapo zinthu monga maukwati a amuna okhaokha komanso ena a akazi okhaokha kapena kuloleza zithunzithunzi ndi makanema olaula. Mutharika anaitanitsa mafumu 158 kunyumba yachifumu ya Sanjika pa 12 chaka chino komwe atsogoleriwo akuti adati Mutharika akane ganizo la IMF. Iye adatanitsanso abusa omwenso ati adagwirizana ndi ganizo lokana kutsitsa mphamvu ya kwacha. ",2 " Uve ndi gwero la linyonyo Mkulu wa bungwe la Heart to Heart Foundation(HHF) mboma la Machinga Derlings Phiri wati gwero la matenda a linyonyo ndi uve. Malingana ndi Phiri, linyonyo ndi matenda a maso omwe munthu akalekerera kwa nthawi yaitali amayambitsa khungu. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kusamba kumaso ndi sopo kumathandiza kupewa linyonyo Iye adafotokoza kuti kukanda kapena kugwira mmaso ndi mmanja mosatsamba kumaika maso pa chiopsezo cha linyonyo chifukwa mmanja mwa uve mumakhala tizilombo tingonotingono toyambitsa matendawa. Ndi bwino kuti nthawi zonse anthu azisamba mmanja ndi sopo akachoka ku chimbudzi, akamaliza kusintha ana matewera komanso akagwira chinthu china chilichonse asanagwire mmaso mwao, adatero Phiri. Mkuluyu adati anthu akaona zizindikiro za matendawa monga kutuluka misonzi pafupipafupi, kuyabwa, kufiira maso ndi zizindikiro zina azithamangira ku chipatala kuti akapimidwe ndi madotolo. Osathira mankhwala a zitsamba mmaso chifukwa zina zimakhala dziphe zomwe zikhoza kuononga maso, adatero mkuluyu. Phiri adati ngakhale linyonyo limagwira munthu wina aliyense, limayala maziko kwambiri pa ana. Iye adati izi zimakhala chomwechi chifukwa ana nthawi zambiri amasewera pa fumbi ndi malo ena omwe amakhala ndi tizilombo toyambitsa matendawa makamaka ngati sakumbukira kusamba mmanja asadakande mmaso. Ndi udindo wa makolo kuphunzitsa ana kuti azikupewa kukanda mmaso ndi mmanja mwa uve kuti linyonyo litheretu mdziko muno, adatero mkuluyu. Phiri adaphera mphongo potsindika kuti munthu wina aliyense azisamba kumaso ndi sopo akangozuka chifukwa manthongo amaitana tizilombo toyambitsa linyonyo. ",6 "Mzika ya Dziko la Ghana Injatidwa Itapezeka ndi Mankhwala Ozunguza Bongo Wolemba: Thokozani Chapola adiomaria.mw/wp-content/uploads/2019/10/ADARKWA.jpg 607w"" sizes=""(max-width: 240px) 100vw, 240px"" />Wapezeka ndi mankhwala ozunguza bongo-Adarkwa Apolisi ku bwalo la ndege la Kamuzu mu mzinda wa Lilongwe amanga mayi wina wa mdziko la Ghana kaamba kopezeka ndi mankhwala ozunguza bongo otchedwa Apomorphine. Mneneri wa apolisi ku bwalo la ndegeli Sub Inspector Sapulani Chitonde watsimikiza za nkhaniyi polankhula ndi Radio Maria Malawi. Mankhwala ozunguza bongo otchedwa Apomorphine omwe apezeka ndi mayiyo Iye wati mayiyu Sally Adarkwa wa zaka 45 zakubadwa anafika mdziko muno masiku anayi apitawo ndipo lero ndi pomwe amabwelera mdziko la kwawo koma atafika pa bwalo la ndegeli apolisi anamupeza ndi mankhwalawa omwe ndi olemera 5.2 kilograms. Mayiyu yemwe amayembekezeka kukwera ndenge ya south african airways ananjatidwa pa malo a chipikisheni omwewo ndipo akawonekera ku bwalo la milandu posachedwapa. Izi zikudza patangopita maola khumi ndi awiri, apolisi omwewanso atamanga mzika ya dziko la Nigeria pamene imafuna kudutsitsa mankhwala ozunguza bongo otchedwa Cocaine. Padakalipano mkulu wa apolisi woona za mabwalo a ndenge a Mabvuto Chiumbuzo achenjeza anthu kuti mabwalo a ndege si malo odusitsira zinthu zosayenera. ",7 " Ndithu chili ndi mwini Kusankha Balaba Kumukana Yesu Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Usapange mistake, chonde chonde Nyimbo ya Evans Meleka idali kuphulika pa Wenela tsiku limenelo. Ya Ndirande iyi! Machinjiri inayo! Za Lilongwe mpaka ku Area 18 mwinamo! Koma abale anzanga, ngati pali dera limene latchuka zedi zaka zimenezi ndiye ndi Area 18. Pajatu nanenso mizu yanga ili ku Upper Area 18, inde kuja kwa Senti! Chomwe ndimadabwa nchoti akaphika nsima imakoma ngati muli kale soya pieces. Abale soya akanakhalako ndi khalidwe. Akanangosankha chimodzi. Soya yemweyo ena akukonza mkaka. Soya yemweyo ena akukonza masoseji! Akanakhala ndi khalidwe soyayu. Kumukana Yesu Kufuna Balaba! Nyimboyi idavuta kwambiri pa Wenela tsiku limenelo potengera ndi zija zidaachitika kwa Chinsapo. Atitu kumeneko chigandanga china chotchedwa Balaba chidaphedwa nkuvulidwa chinochino. Ya Ndirande iyi! Ya Machinjiri iyo! Ya ku Area 18 inayo! Mkulu anali oopsa uyu. Ngakhale apolisi amamuopa, moti anthu akakanena kupolisi kuti Balaba akuwasautsa, apolisiwo amaneneratu kuti mukamugwira Balaba mumubweretse kuno. Mpake anthuwo anamupititsa Balaba wakufa kupolisiko, adatero Abiti Patuma. Kusankha Balaba Kumukana Yesu Usapange mistake, chonde chonde! Ndipo ndangomva kuti mkulu wina wa kampani ya alonda wapeza tender yolondera polisi ya pa Wenela. Koma zisatikhudze, adatero wa pamalopo, Gervazzio. Gervazzio adayatsa kanema. Padali MBC-TV ndipo adabwera Jeffrey Kapusa. Adali kuulutsa nkhani ya mwana wina amene adagwiriridwa ndipo apolisi komanso amene amayenera kumuthandiza ena sanatero, msungwana kumangolira. Anthu ogwirira anawa tikadatha kuwatchula kuti zitsiru, koma sititero chifukwa mawuwo siwoyenera kuwatchula pagulu. Choncho tingoti ndi wopusa. Si zitsiru ayi, Kapusa adali kutero. Mr Splash! Mawu ake ali mkamwa, adatulukira Moya Pete. Ndakwiya khwambiri. Anthu inu ndi zitsiru! Ndinu zitsiru kwambiri! Zitsiru zakumwa madzi wochapira ndevu, adali kutero Moya Pete. Kenako, adatenga cholembera, nkulemba pamalaya a Gervazzio: Chitsiru. ",15 " Zipani zikufuna mayankho pa zitupa za unzika Zipani za Malawi Congress Party (MCP) ndi Peoples Party (PP) zati kusowa kwa zitupa zina za olembetsa mkaundula wa unzika zidzasokoneza chisankho cha patatu cha 2019. Nthambi ya National Registration Bureau (NRB) yati mwa zitupa 1.7 miliyoni zomwe zidajambulidwa mgawo loyamba la zitupa za unzika, 1.5 miliyoni ndizo zatuluka. Izi zili choncho, bungwe loyendetsa chisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) lati lidzagwiritsabe ntchito zitupazo polembera ovota. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mlembi wa PP Ibrahim Matola adati zitupazo sizimayenera kugwiritsidwa ntchito mkalembera wa ovota chifukwa ntchitoyi siyinakhazikike. Tangoyamba kumene ntchitoyi. Tisayidalire ayi bola mtsogolomu zikadzagwira msewu koma padakalipano tiyeni tigwiritse ntchito njira yomwe timagwiritsa nkale lonse, adatero Matola. Mneneri wa chipani cha MCP Eisenhower Mkaka adati zitupa za unzika zokha sizikuyenera kugwiritsidwa ntchito pa mavoti chifukwa zina zikusowa. Kudzazigwiritsa ntchito limodzi ndi zitupa zovotera osati pazokha ayi poopa libolonje, adatero iye. Phungu wa ku mmawa kwa boma la Dowa, Richard Chimwendo-Banda wa MCP, adati kufaifa kwa zipangizozo kukhoza kuchititsa kuti anthu ambiri mchigawo cha pakati asadzakhale ndi zitupa ndikulephera kudzaponya nawo voti. Mkaka: Alongosole Mneneri wa MEC Sangwani Mwafulirwa watsindika kuti zitupazo zidzagwiritsidwa ntchito popanga kaundula wa odzavota pa chisankho cha 2019. Munthu amene adzakhale ndi chitupa, nzachidziwikire kuti ndi nzika ndiye sitidzalimbana naye zambiri komabe tidzaona momwe tidzathandizire omwe alibe zitupa, adatero Mwafulirwa. Iye adati MEC ikuyembekezeka kudzayamba kukonza kaundula wa odzavota ndipo akukhulupilira kuti pofika nthawi yamavoti, nzika iliyonse idzakhala italandira chitupa chake. Mneneri wa nthambi ya NRB Norman Fulatira wati anthu asakhale ndi nkhawa pankhaniyo chifukwa zivute zitani, Amalawi onse adzakhala ndi zitupazo. ",11 " Abwatika bwalo, Polisi ku mangochi Fisi adakana msatsi. Mayi yemwe adauza abale kuti mwamuna wake amafuna kugulitsa mwana wawo wa chialubino wasintha Chichewa. Vanessa Manyowa wauza bwalo la milandu ku Mangochi kuti zomwe adanenazo zidali zopeka chifukwa panthawiyo nkuti atayambana ndi mwamuna wake pa nkhani za kumunda. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kadadzera: Nzokhumudwitsa Mayiyo adabereka mwanayo wa chialubino asadakwatiwe ndi mwamuna wake watsopanoyu. Padakali pano mwanayo ali ndi zaka 14. Nkhaniyo idachitika mwezi watha pamene Manyowa adauza achimwene ake kuti mwamuna wake, Nick Adams, wa zaka 38 amafuna kugulitsa mwanayo. Achimwenewo adatengera nkhaniyo ku polisi ya Mangochi moti Adams adamangidwa ndi mlandu woganiziridwa kugulitsa mwana wa chialubino. Lachinayi sabata yatha nkhaniyo adaitengera ku khoti la mbomalo komwe Manyowa adasintha Chichewa. Manyowa adauza bwalolo kuti adapeka nkhaniyo atayambana ndi mwamuna wakeyo chifukwa adamukaniza kutengapo gawo lake la chimanga ndi mtedza womwe akolola. Ndazindikira kuti ndidalakwitsa kwambiri. Mwamuna wanga sadanenepo zoti akufuna kugulitsa mwana wathu, Manyowa adauza bwalo. Izitu zidachititsa Manyowa ndi achimwene ake apemphe bwalolo kuti mlanduwo utsekedwe. Woweruza mlanduwo, Joshua Nkhono adadzudzula Manyowa popekera mwamuna wake nkhani. Nkhono adati nkhani zokhudza anthu achialubino nzovuta choncho mayiyo adalakwitsa. Apa woweruzayo adathetsa mlanduwo, koma adanenetsa kuti bwalo lilanga aliyense wopeka nkhani zokhudza anthu achialubino. Nawo apolisi ati ndiwokhumudwa kaamba koti Manyowa adawapusitsa. Mneneri wa apolisi mdziko muno James Kadadzera adati zomwe wachita Manyowa nzobwezeretsa zinthu mmbuyo. Kadadzera adati palibe chomwe apolisi angachite chifukwa mlandu watha. Polankhulapo mtsogoleri wa bungwe la anthu oyimira anzawo pa milandu la Malawi Law Society (MLS) Burton Mhango adati Manyowa ali ndi ufulu wotseketsa mlandu. Iye adati zimatengera kukula kwa mlanduwo, komanso umboni womwe ulipo. Pankhaniyi zikuonetsa kuti wodandaula yemwenso akadakhala mboni yaikulu ndi yemwe adafuna kuti mlanduwo utsekedwe, choncho ngakhale apolisi akadafuna kuti upitirire sizikadaphula kanthu chifukwa pakadakhala popanda mboni. Mlandu wopanda mboni umavuta, adatero Mhango. Koma Mhango adati zomwe wachita Manyowa zaika pachiopsezo moyo wa mwana wake chifukwa anthu akudziwa komwe akupezeka ndipo ena oyipa moyo akhoza kumuchita chipongwe. Choncho Mhango adapempha aboma kuti apereke chitetezo chokwanira kwa mwanayo kuti ambanda asalowererepo. ",7 " JB asankha Kachali Mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda Lachitatu adasankha Khumbo Kachali kukhala wachiwiri wake. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Kachali, yemwe ndi phungu wa ku Mzimba, ndi wachiwiri kwa Banda mchipani cha Peoples Party (PP). Kachali ndi wachinayi kukhala paudindowu kuchokera pomwe dziko lino lidayamba ndale za zipani zambiri mu 1994. Mmbuyomu, Justin Malewezi, Cassim Chilumpha ndi Banda adakhalapo paudindowu. Kusankhidwa kwa Kachali kudadza tsiku limene Banda adasuntha mlembi wamkulu muofesi ya mtsogoleri wadziko lino ndi nduna zake woona za madyedwe ndinso za HIV Dr Mary Shawa kupita kuunduna woona za amayi. Maudindo ambiri akhala akusinthidwa msabatayi kutsatira imfa ya mtsogoleri wakale wadziko lino Bingu wa Mutharika, yemwe adamwalira pa 5 Epulo kunyumba ya boma ku Lilongwe atadwala nthenda ya mtima. Thupilo adalitengera kuchipatala cha Kamuzu Centre mumzinda wa Lilongwe koma malinga ndi malipoti achipatala akuti Mutharika adali atamwalira kale pomwe amafika kuchipatalako. Madzulo a Lachinayilo, boma lidati Mutharika amutengera ku KCH komwe adati akudwala mtima. Lachisanu pa 6 mtsogoleri wakale wa dziko lino, Bakili Muluzi komanso Banda adachititsa msonkhano pomwe adati malamulo adziko lino akuyenera kutsatidwa pa yemwe alowe mmalo mwa Mutharika ngati iye wadwalika kapena wamwalira. Lachisanu lomwelo cha mma 11 koloko usiku, akuluakulu ena aboma monga Patricia Kaliati, Nicholas Dausi, Kondwani Nankhumwa, Symon Vuwa Kaunda adachititsa msonkhano wa atolankhani ku Area 4 mumzinda wa Lilongwe. Pa msonkhanowo, Kaliati adatsutsa zomwe Muluzi komanso Banda adanena ndipo adati Banda sakuyenera kukhala mtsogoleri chifukwa adachoka mchipani chomwe chimalamulira cha DPP ndikukayambitsa chipani chake cha PP. Kaliati adakananso kuti sanena momwe Mutharika akupezera koma adangoti ali ku chipatala cha Milpark mdziko la South Africa. Apa nkuti nyumba zoulutsira mawu zamaiko ena zitalengeza kuti Mutharika wamwalira. Mmawa wa Loweruka Ofesi ya Pulezidenti ndi Nduna idalengeza kuti Mutharika wamwalira ndipo idati Amalawi akhuza malirowo kwa masiku khumi. Lowerukalo, yemwe adali wachiwiri kwa mtsogoleriyu, Joyce Banda adalumbiritsidwa kukhala mtsogoleri wa dziko lino. Mutharika yemwe adali mwana wa mphunzitsi adabadwa mu Febuluwale 1934 ndipo amachokera mmudzi mwa Kamoto mboma la Thyolo. Mutharika dzina lake adali Ryson Webster Thom ndipo adasintha dzinali mzaka za mma 1960. Malemuwa omwe adali katswiri pa zachuma adasankhidwa kukhala mtsogoleri wa dziko la Malawi mu 2004 kukhala mtsogoleri wa dziko lino ataimira chipani cha UDF. ",11 " Akufuna wogwirizira ufumu achoke, apepese Mafumu mdziko muno agwirizana ndi ganizo la mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda kuti magulupu ndi nyakwawa asiye kulandirira ndalama kubanki. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Banda adalankhula izi sabata yatha pasukulu ya Nsumwa mboma la Salima poyankha pempho la mfumu Ndindi kuti mafumu akuvutika pokalandirira ndalama kubanki. Polandira Banda, Ndindi adati ndondomeko yomwe idayambitsidwa mboma la chipani cha DPP kuti iwo adzikalandilira mswahala kubanki yazunza mafumuwa ponena kuti ndalamayo imathera ulendo. Apa Banda adati nyakwawa ndi magulupu asamakalandirirenso ndalama kubanki ponena kuti ndondomeko yapoyamba ibwezeretsedwa. Apa mafumuwa ati nkhaniyi iwathandiza chifukwa ndalamayo samaiwona ubwino wake malinga nkuti komwe kuli mabanki ndi komwe amakhala ndi mtunda wautali. Nyakwawa Kapoti ya kwa T/A Zilakoma mboma la Nkhata Bay yati kuchokera mmudzimo kukafika kuboma komwe kuli mabanki ndi mtunda omwe amalipira K2 000 kupita ndi kubwera. Mfumuyi yauza Tamvani kuti penanso akapita ndalamazo amakapeza zisadalowe. Ndimalandira K2 500 ndipo ndimaononga K2 000 kusonyeza kuti malipiro anga ndi K500. Apa tiyamike kuti tizilandira kumudzi kuno, idatero mfumuyo. Gulupu Chisinkha ya mboma la Mulanje kwa T/A Mabuka yati mfundo ya boma ili bwino bolani ndalamazo adziwapatsadi. Ndondomeko yapoyambayonso idali ndi mavuto ake pomwe pena malipiro sitimalandira. Ganizoli nlabwino bola tizilandira, adatero Chisinkha. Mtsogoleri wakale wa dziko lino, Bingu wa Mutharika ndiye adalamula kuti aliyense wogwira ntchito mboma kuphatikiza mafumu adzikalandira malipiro awo kubanki. ",8 " Maliro pa chisangalalo Mwambo wa chikondwerero choti dziko lino latha zaka 53 lili pa ufulu wodzilamurira lidasanduka chisoni pomwe ana 7 ndi bambo mmodzi adamwalira pokanganirana kulowa mbwalo la za masewero la Bingu National Stadium kumene kumayenera kuchitika mpira waulere. Izi zidadziwika pomwe mtsogoleri wa dziko lino adatsogolera Amalawi pa mapemphero wolingalira za ufuluwo ku Bingu International Convention Centre (BICC) pomwe woyendetsa mwambowo mbusa Timothy Nyasulu adalengeza za omwalirawo. Iye adapempha anthu kuti akhale chete kwa mphindi imodzi polemekeza mizimu ya omwalirawo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Wapolisi kuthandiza mmodzi mwa ana ku BNS Ndipo nduna ya zamalonda ndi mafakitale Joseph Mwanamvekha, yemwenso adali wapampando wa komiti yoyendetsa mwambowo, adatsimikiza za imfa ya anthuwo mapemphero ali mkati. Iye adati anthu oposa 40 adavulala pangoziyo. Nthambi yofalitsa nkhani za boma lidati anthu 65 adamwalira. Mutharika ndi mayi Gertrude Mutharika adakazonda anthu amene adavulala pa chipwilikiticho ku Kamuzu Central Hospital. Mutharika adati :Boma ndi lokonzeka kuthandiza pangoziyi. Dziko la Malawi limakumbukira kuti latha zaka 53 kuchokera pamene mtsogoleri wa dziko lino Dr Hastings Kamuzu Banda adakwanitsa kupeza ufulu kuchokera kwa Angerezi amene adayamba kulamulira dziko lino mzaka za mma 1890. John Chilembwe, mmodzi mwa Amalawi oyambirira kufuna kumenyera ufuluwo adamwalira mu 1915. Zikondwerero za chaka chino zinalipo kuyambira Lachitatu pa 5 July pomwe asilikali ndi achitetezo ena adayenda mmizinda ya Blantyre, Zomba ndi Mzuzu. Ndipo chikondwerero chimayenera kufika pa mponda chimera pa masewero a Nyasa Big Bullets ndi Silver Strikers amene amayembekezeka kuchitika kumalo a ngoziyo. Komatu galimoto za chipatala ndi zapolisi zidali kukangalika kuthandiza ovulala pa zisawawazo. Koma polankhula ndi Tamvani zisangalalozo zisanachitike, Amalawi ena adati ngakhale dzikoli latha zaka 53 likudzilamulira maloto ena amene adalipo pomenyera ufulu wa dziko lino. Yemwe adakhalapo sipikala wa Nyumba ya Malamulo, Sam Mpasu adati mMalawi wa zaka 53 ali panayi: Zina zasintha pangono, zina sizinasinthe, pomwe zina zaima kapena kubwerera mmbuyo. Iye wati kunena mosapsatira zaka 53 sizidabweretse kusintha kwenikweni paulamuliro ndi kayendetsedwe ka maufulu a anthu mdziko muno. Mwa zina, iye adati ulamuliro wa Kamuzu Banda udayesera kubwezeretsa ulimi mchimake pamene adakhazikitsa makampani otulutsa zinthu zina kunja zimene mu ulamuliro wa atsamunda zimakapangidwa kunja, koma zina sizikuyenda. Adapereka zitsanzo za makampani a Sucoma, yomwe inkakonza shuga, Malawi Cotton yomwe inkaomba nsalu komanso British American Tobacco yomwe inkapanga ndudu ngati zina mwa zotsimikiza izi. Dziko lino lisanaladire ufulu, Mpasu adati zonsezi zinkabwera kuchokera kunja, ngakhale alimi ochuluka amene ankazilima mdziko muno ankatumiza kunja chifukwa adali Atsamunda. Kamuzu adayesetsanso kulimbikitsa msika wa mbewu kudzera ku Admarc ndipo adaonetsetsa kuti manyamulidwe a mbewu ngosavuta chifukwa kudali sitima za panjanji zomwe zimanyamula katundu pa mtengo otsika kupita ku misika, watero Mpasu. Ndipo mkulu wa bungwe loyanganira za momwe maphunziro akuyendera mdziko lino George Jobe wati pakutha pa zaka 53, Malawi amayenera kukhala ndi ntchito za umoyo za pamwamba motsatira chiyenerezo cha bungwe lalikulu loyanganira zaumoyo la World Health Organisation (WHO) koma mmalo mwake zinthu zambiri sizikuyenda. Mpaka pano sitidayambe kukwaniritsa mlingo wa WHO oti K15 pa K100 iliyonse mbajeti izikhala ya za umoyo. Chiwerengero cha ogwira ntchito za chipatala chikadali chotsika kwambiri poyerekeza ndi anthu omwe dokotala mmodzi amawona pa tsiku, watero Jobe. Ndipo kupatula zaumoyo, mkulu wa mgwirizano wa mabungwe a zamaphunziro, Benedicto Kondowe wati sizoona kuti zaka 53 zingathe ana asukulu makamaka a kuma Yunivesite nkumakhala pakhomo miyezi yambiri chifukwa cha mavuto msukulu zawo. Iye wati pa zaka zonsezi, atsogoleri amayenera kukhala atapanga njira zothandizira kuti kalendala ya sukulu kuyambira ku pulayimale mpaka ku Yunivesite isamasokonekere chifukwa kutereku nkulowetsa maphunziro pansi. Posachedwapa, aphunzitsi adali pa sitalaka pa nkhani ya maphunziro ndipo tikunena pano ophunzira mma Yunivesite sadatsegulire chitsekereni miyezi ingapo yapitayo nkhani yake kayendetsedwe, adatero Kondowe. ",1 "Sapereka chithandizo Agogo, Ndine mtsikana wa zaka 21 ndipo ndili ndi mwana mmodzi. Amuna anga adandisiya ataona kuti ndili ndi pathupi ndipo mwana atabadwa adauzidwa koma mpaka pano sadabwereko kudzaona mwana wawo. Ndikawauza za chithandizo samayankha, amangozengereza. Chomvetsa chisoni nchakuti munthune ndimakhala ndi agogo okalamba poti makolo anga onse adamwalira. Ndithandizeni, ndipange bwanji? Pepa mtsikana, Apa zikuonekeratu kuti ngakhale ukuti amuna anga anthunu simunali pabanja ngakhale mumagonana mpakana kuberekerana mwana. Chimene chimachitika nthawi zambiri nchakuti atsikana akangogwa mchikondi ndipo mwamuna akangowauza kuti awakwatira, basi amaganiza kuti mwamuna ndi yemweyo basi ndipo amayamba zogonana naye ati pofuna kulimbikitsa chikondi kuti asamakaike za chikondi chawo, kumene kuli kulakwa kwakukulu. Atsikana ambiri aononga tsogolo lawo chifukwa cha mchitidwe wotere chifukwa anyamata kapena amuna ambiri ndi akamberembere, ongofuna kudzisangalatsa osalabadira za tsogolo la mnzawo. Akangomva kuti mtsikana watenga pathupi basi, chibwenzi chimathera pomwepo. Zikatero mtsikana zako zada. Koma dziko lino lili ndi malamulo okhudza maukwati ndipo ngati wina wakuchimwitsa, ali ndi udindo woti akusamale komanso mwana. Ndiye apa usazengerezepita ukadule chisamani kukhoti basi kuti chilungamo chioneke. Mwina amuna ena amene amakonda kuchimwitsa ana a eni akhoza kutengerapo phunziro! Ndinamugwira chigololo Anatchereza, Ndakhala pabanja zaka 25 ndipo ndili ndi ana anayi. Mwatsoka tsiku lina ndidapezerera akazi akuchita chigololo ndi mwamuna wina koma adathawa kotero kuti sindidathe kumulanda china chilichonse ngati umboni ndipo pachifukwa ichi mlandu sudandikomere, amfumu adagamula kuti nkhani yanga ndi yopanda umboni choncho banja siliyenera kutha. Ine kubanjako ndidachokako koma mkazi wangayo akumapepesa kuti ndimukhululukire. Ndithandizeni, nditani pamenepa? Achimwene, Pepani ndithu kuti banja lanu lagwedezeka chifukwa cha kusakhulupirika kwa akazi anu. Kukhala mbanja zaka 25 si chapafupi ndipo kuti lero ndi lero banja lithe chifukwa choti wina wapezeka akuchita chigololo ndi chinthu chomvetsa chisoni zedi, makamaka chifukwa angavutike kwambiri ndi ana osalakwa. Kodi, achimwene, mumapephera? Ndafunsa choncho chifukwa ngati mumakhulupirira Mulungu, mawu ake kudzera mwa mwana wake Yesu Khristu, amatiphunzitsa za kukhululukira anzathu akatilakwira, osati kamodzi kapena kawiri kokha, ayi, koma maulendo 77 kuchulukitsa ndi 7 (77 x 7). Kodi inuyo mukufuna kunena kuti simudachimwepo ndi mkazi wina kapena mkazi wamwini chikwatirireni? Mwina mudachitapo chigololo koma simunagwidwe chabe! Ndiye apa, poti mkazi wanu wagwira mwendo kuti mumukhululukire, ine pempho langa ndi loti mutero ndithu, munthu salakwira mtengo, koma munthu mnzake. Ngati Mulungu amatikhululukira tikamuchimwira, ife ndani kuti tisakhululukire mnzathu akatilakwira? Mwachoka, kutali limodzi, chonde ganizani mofatsa. Komabe ndi mmene kunja kwaopsera masiku ano ndi mliri wa HIV/Edzi, ndi bwino ngati mungabwererane kuti mukayezetse magazi musanayambe kukhalira malo amodzi kuti mudziwe mmene mthupi mwanu mulili. n ",15 " Kuli zionetsero pa 13 December Lachitatu pa 13 December kukhala ali ndi mwana agwiritse mzigawo zonse zitatu za dziko lino pamene bungwe la mipingo la Public Affairs Committee (PAC) litsogolere zionetsero. Izitu ndi zionetsero zokakamiza boma kuti libweretse mabilo okhudza za chisankho mu Nyumba ya Malamulo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Chilima (R) adawerenga kalata Mabilowo, mwa zina, akukamba kuti mtsogoleri wa dziko azisankhidwa ndi mavoti oposa 50 peresenti. Sinodi ya mpingo wa CCAP ku Livingstonia ndi sukulu ya ukachenjede ya Mzuzu apsepserezera zionetserozi posindika kuti patsikuli akayenda ku msewu. Mbusa Levi Nyondo wati PAC ikulankhula zenizeni kotero nkofunika kuthandizana nayo pa nkhondo yokakamiza boma. Mamembala onse ampingo akupemphedwa kuti apite kumsewu kukachita zionetserozo, adatero Nyondo. Lamulungu lathali, wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Saulos Chilima adawerenga kalata ya mpingo ku Parish ya St Patrick mu mzinda wa Lilongwe yomwe imapempha Amalawi kutengapo gawo pa ziwonetserozo. ",11 "Dayosizi ya Dedza Yati Akhristu Ake Adzipemphelera Panja Mpingo wa katolika mu dayosizi ya Dedza wapempha akhristu ake kuti adzichita miyambo ya nsembe za Misa panja pa tchalitchi ngati njira imodzi yopewera mliri wa Coronavirus. Malingana ndi kalata yomwe yatulutsidwa dzulo pa 6 July ndipo yasainidwa ndi mkulu owona za utumiki mu dayosiziyi bambo Peter White, izi zadza kaamba kofuna malo opemphelera otakasuka pofuna kuchepetsa kufala kwa nthendayi. Akuti anthu azipemphera panja pa tchalitchizi Bambo White ati ngakhale pali mavuto ena omwe ngadze kaamba kopemphera panja, akhristu akuyenera kupilira kusiyana ndi kuti atenge nthendayi. Milungu ingapo yapitayi tinawona kuti matchalitchi athu akutsatira zomwe a chipatala akunena koma chifukwa cha kuchepa kwa malo a mtchalicthi, anthu sakumakhala motalikirana ndipo apa ndi pomwe tinakhala pansi ndi kuona kuti akhritsu azisonkhana panja pa tchalitchi popeza kuti pali malo aakulu, anatero bambo White. Iwo ati pamene amapanga chiganizo chimenechi anaganiziranso mavuto omwe akhristu azikumana nawo maonga mphepo komanso kakhalidwe ka malo a panjapo komabe iwo ati akhristuwa akuyenera kupilira kusiyana ndi kuti atenge nthendayi kaamba kothithikana mtchalitchi. ",13 " kwa Ngombe zamkaka zimalira chisamaliro chokwanira Lasford Mbwana ndi mmodzi mwa alimi a ngombe zamkaka omwe akuchita bwino kwambiri kwa Bvumbwe mboma la Thyolo. Moti mlimiyu akuyenda chokhala kaamba koti adagula galimoto kuchokera mu ulimiwu. BRIGHT KUMWENDA adacheza naye motere: Tafotokozani, kodi ulimi wa ngombe zamkaka mudayamba liti? Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ulimi wa ngombe zamkaka ndidayamba 2006 nditaona momwe anzanga amapindulira. Moti ngombe yanga yoyamba ndidagula K130 000 ndipo ndakhala ndikuonjezera mpaka zidafika 8. Kodi mwapindula motani ndi ulimiwu? Mbwana kudyetsa ngombe zake zizipereka nkaka wochuluka Phindu ndi losachita kunena. Ndikadakhala kuti sindikupindula sindikadaonjezera chiwerengero cha ngombe zanga. Ngombe za mkaka zimandipatsa ndowe zothira kumunda, ndalama zogulira chakudya, zovala ndi zinthu zina zosoweka pabanja panga. Panopa banja langa likuyenda chokhala chifukwa choti tidagula galimoto kuchokera mu ulimi womwewu. Nanga mungamulangize zotani munthu amene akufuna kuyamba ulimi wa ngombe zamkaka? Choyamba akhale ndi ndi chidwi ndi ziweto, malo wobzala nsenjere, amange khola labwino, akhale pafupi ndi madzi, komanso msika wa mkaka. Kodi mukati khola labwino mukufuna kunena chiyani? Khola labwino limakhala ndi malo wodyera, wokamira mkaka, womwetsera mankhwala, wosewerera, wokhalira mwana akabadwa, woti ngombe izikhala panthunzi ikafuna kupuma kapena kugona. Kodi patsiku mumakama mkaka wochuluka motani? Ngakhale ndili ndi ngombe 8 ndikukama zinayi zokha chifukwa choti zina ndi zazingono. Udzu, deya ndi masese zikamapezeka mosavuta ndimakama malita osachepera 100 patsiku omwe amandipatsa ndalama zokwana pafupifupi K500 000 pamwezi. Chinsinsi choti ngombe izitulutsa mkaka wambiri nchiyani? Kudyetsa mokwanira, komanso mtundu wa ngombezo. Ngombe sizisiyana ndi munthu. Kodi simukudziwa kuti mayi akamadya mokwanira mwana wake amasangalala chifukwa choti mkaka umatuluka wambiri? Ngombe zamakono zimatulutsa mkaka wambiri pofanizira ndi zachikaladi. Mukati ngombe zachikaladi mukufuna kutanthauzanji? Ukapereka umuna wa ngombe za Chizungu kwa ngombe zachikuda za Malawi Zebu, ana obadwa amakhala makaladisakhala azungu kapena achikuda. Amakhala a pakatikati. Moti mkaka omwe amatulutsa sukhala wambiri ngati wa ngombe ya Chizungu, komanso sukhala wochepa kwambiri ngati wa yachikuda. Kodi ngombe zanu ndi za mtundu wanji? Ngombe zanga ndi za mtundu wa Holstein. Alimi ambiri a ngombe za mkaka mdziko muno akuweta ma Holstein, Jersey kapena ma Friesian. Tafotokozani, kodi mumagula kuti ngombe zamkaka? Timagula kwa alimi anzathu. Ena amagula mmafamu a boma monga ku Mikolongwe ku Chiradzulu, Likasi ku Mchinji, Diamphwi ndi Dzalanyama ku Lilongwe ndi Dwambadzi ku Mzimba. Mabungwe a alimi a ngombe zamkaka a Shire Highlands Milk Producers Association (Shmpa), Central Region Milk Producers Association (Crempa) ndi Mpoto Dairy Farmers Association (MDFA) amathandizanso alimi kupeza ngombe zamkaka. Nanga munthu asungire zingati akafuna kugula ngombe zamkaka? Zimatengera ndi wogulitsa, komanso komwe ukukagula ngombezo. Alimi ambiri amagulitsa ngombe pamtengo wapakati pa K250 000 ndi K300 000. Ikakhala yabere imafika mpaka K400 000. Ndi mavuto otani omwe alimi a ngombe zamkaka amakumana nawo? Kusowa kwa madzi ndi zakudya makamaka miyezi ya pakati pa October ndi April. Nthawi imeneyi deya amasowa, komanso udzu umavuta kuwupeza. Moti alimi amayenda mitunda italiitali kuti apeze udzu wodyetsa ngombe zawo. Chaka chathachi thumba la deya tim0agula K6 000. Ngakhale adali wokwera mtengo, amavuta kupeza. Kuthimathima kwa magetsi kumawononga mkaka. Alimi a ngombe zamkaka amapanga magulu osiyanasiyana (bulking groups) omwe amasunga mkaka wawo mmalo ozizira, kudikira makampani kuti adzagule mkakawo. Magetsi akathima, mkaka ndi kuwonongeka asadadzautenge ndiye kuti alimi ali mmadzi. Kuphatikizira apo, mitengo yomwe makampani amatigulira mkaka ndi yotsika kwambiri. Ulimi wa ngombe zamkaka susiyana ndi wa fodya chifukwa wogula ndi amene amayika mtengo. Ndi matenda otani omwe amagwira ngombe? Chifuwa chachikulu, chigodola, zotupatupa ndi ena mwa matenda omwe amazunza ngombe. Nanga mawu anu otsiriza ndi wotani? Potsiriza ndikufuna ndipemphe anzanga kuti akumbe zitsime ndi kubzala nsenjere kuti asamavutike kupeza madzi ndi chakudya mudzinja. ",4 " Tikolola chimanga chochulukaNduna Nduna ya zamalimidwe komanso kuonetsetsa kuti mdziko muno muli chakudya chokwanira, Peter Mwanza yati undunawu ukulosera kuti chaka chino dziko lino likolola chimanga chochuluka ndikukhala ndi china chapadera. Polankhula Lachitatu mumzinda wa Lilongwe pomwe amafotokozera atolankhani za kholola wa chaka chino, ndunayi yati malinga ndi zolosera dziko lino lingapate matani 740 000 a chimanga apadera. Chaka chatha dziko lino lidapeza matani oposa 500 000 apamwamba. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Zolosera za ndunayi zikudza pomwe zadziwika kuti Dedza ndi madera ena kuchigawo cha kumpoto kwa dziko lino mvula yachita njomba ndipo alimi ali pachiopsezo kuti mwina galu wakuda awayendera kumeneko. Ngati zoloserazo zingatheke ndiye kuti dziko lino likhala ndi chakudya chambiri chapadera chifukwa dziko lino limafuna matani achimanga 2.6 miliyoni. Mwanza adati ichi ndi chisonyezo chabwino kuti dziko lino lapata chimanga chambiri chapadera ndipo adati boma liyesetsa njira ya zipangizo zotsika mtengo kuti dziko lino lipate chakudya chambiri. Mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda polankhula atangokwanitsa chaka akulamulira ku Lilongwe adati madera omwe akhudzidwa ndi njala ndi ochepa kotero boma liyesetsa kuti ulimi wa mthirira uyambike kuti njala ithe mdziko lino. Mu 2012 dziko lino lidapeza matani 3.624 miliyoni a chimanga ndipo chapadera adali matani 566 552 pomwe mu 2011 tidakolola matani 3.8 miliyoni ndi chapadera matani 1.2 miliyoni. Padakali pano boma kudzera mwa Banda lalengeza kale kuti ndondomeko ya makuponi ipitirira ndipo anthu omwe adzalandire makuponiwa ndi 1.5 miliyoni. Nambalayi idakwezedwa pomwe Banda adayamba kulamula kuchoka pa 1.4 miliyoni. ",4 "President Al-Sisi Akumana Ndi Ziwonetsero Zoyamba Wolemba: Thokozani Chapola mw/wp-content/uploads/2019/09/al-sisi.jpg"" alt="""" width=""524"" height=""366"" />Malamulo atsopano akumulora kulamulira dziko la Egypt mpaka 2030-Al-Sisi Apolisi a mdziko la Egypt agwiritsa ntchito utsi wokhetsa msozi pothamangitsa anthu ena omwe amachita zionetsero zotsutsana ndi ulamuliro wa mtsogoleri wa dzikolo ABDUL FATTAH AL-SISI. Anthuwa ati akufuna kuti Al-Sisi atule pansi udindo wake pomuganizira kuti akukhudzidwa ndi katangale yemwe akuchitika mboma. Malinga ndi malipoti a wailesi ya BBC, ziwonetserozi ndi zoyamba kuchitika chimusankhireni pa udindowu mchaka cha 2014. Padakalipano anthu asanu ndi omwe amangidwa pa ziwonetserozi. Mchaka cha 2013 AL-SISI anatsogolera asilikali a dzikolo pothetsa ulamuliro wa mtsogoleri woyamba mu mbiri ya democracy ya dzikolo MOHAMMED MORSI. Pa chisankho cha mchaka cha 2018 president AL-SISI anapambana ndi 97 percent kaamba koti panalibe munthu wachikoka kwambiri yemwe amapikisana naye. Mwezi wa April chaka chino anthu a mdziko la Egypt anachita voti ndipo anasankha kuti malamulo a dzikolo asinthe kuti athe kulora president AL-SISI kukhala pa udindowu mpaka chaka cha 2030. ",11 " MCP yatiphunzitsa zambiri Nkhani idali mkamwamkamwa miyezi ingapo yapitayi ndi ya msonkhano waukulu wa chipani cha MCP. Zimakaikitsa ngati kumsonkhanowo kukamangidwe mfundo zolemekeza maganizo a anthu. Chikaiko chidakula pamene mphekesera zidali mbweee! Makamaka chipanicho chitalephera kuchititsa msonkhanowo mwezi wa April. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Chikaikocho chidakula zitamveka kuti chipanicho chikufuna kuti anthu ena, makamaka amene angobwera kumene mchipanimo asapikisane nawo pa\mpando wa pulezidenti. Komiti yapadera ndiyo idapereka mwayi onse kuti onse amene adapereka maina awo akhoza kupikisana nawo. Nkhani imodzi imene idatsalira idali yakuti John Tembo, amene malamulo amamuletsa kuti sangaime nawo chifukwa adaimira kale chipanichi kawiri, naye amafuna kupikisana nawo. Koma nthumwi za kumsonkhanowo, zitafunsidwa ngati angakambirane zosintha malamulowo, zidakana kwa mtuu! Wagalu. Izi zikudza pomwe zipani zina monga cha UDF, zidasintha malamulo kuti mwana wa mtsogoleri wakale wadziko lino Bakili Muluzi, Atupele, aimire chipanichi. Poyamba, Atupele sakadapikisana nawo chifukwa malamulo amaletsa kuti amene sadakwane zaka 35 asapikisane nawo. Nthumwi zidasintha malamulowo kuti Atupele aime. Ndipo nthawi yosankha atsogoleri itakwana, nthumwizo zidasankha amene amaoneka ngati alendo kuposa nkhalakale za chipanicho. Izi zikungosonyeza kuti demokalase ya mchipani yayala nthenje mu MCP. Koma chomwe tingalangize atsogoleri a chipanichi kuti akhale okhwima mundale ndi kumulandira Kusakhale kugawanikana monga zidalili Tembo atangogonjetsa Gwanda Chakuamba mu 2003. ",11 " Chalaka Kinnah Tom sangatole Aganyu tidagwiritsidwa utsi titalonjezedwa ndi yemwe anali mphunzitsi wa Flames Tom Santfiet kuti Flames ikavulaza Nigeria. Nigeria idatiumbudza 2-0. Iye adatulutsa Robin Ngalande poseweretsa Atusaye Nyondo yekha kutsogolo ngakhale timaluza. Kodi amatchinjiriza chiyani? Uyutu adali ndi kampeni. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Aganyu zikutiwawabe. Tom wapita atalephera kuchita chomwe chidamuchotsetsa ku Belgium. Ngakhale tikumva kuwawa, Fam ikusangalala chifukwa tathera nambala 2 mgulu lathu. Suzgo Nyirenda ndiye watero. Koma Nyirenda adziwe kuti palibe chosangalalira chifukwa panambalayi sitilandira kanthu komanso sitipita kulikonse. Aganyu tilikhwira Fam chifukwa zonsezi ndi iyo. Uncle Tom adawatenga kuti? Nanga mudadziwana naye bwanji? Mudatsimikizika bwanji kuti angatithandize? Ku Zambia adagonja kwa Angola ndi Zimbabwe. Ku Botswana adakagonjanso 1-0. Nigeria ndi iyo idamukodzetsa akuwonayo. Chanzeru wachita ndikupha Rwanda timu yomwe ndi ananso kwa ife. Tikuona kuti vuto ndi mtima woipa umene udabzalidwa mwa Fam pokhulupirira aphunzitsi akunja. Izi sizingatithandize, mmalo mwake mukuononga timu yathu. Mwatenga Tom koma wachoka atabalalitsa Flames. Joseph Kamwendo, Simplex Nthala adawathamangitsa ku timuyi. Sitikufuna tiyambe kuliriranso Kinnah Phiri chifukwa adachotsedwa akumanga timu. ",16 " Womuganizira kutaya khanda lake anjatidwa Anthu okhala mdera la Hilltop mmzinda wa Mzuzu adadzidzimuka Lamulungu lapitali, mayi wina wapabanja wochokera mderali atadziwika kuti adataya mwana mchimbudzi chokumba. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Malinga ndi anthu ozungulira nyumba ya Taona Chonga, wochokera mmudzi mwa Mzukuchonga, mboma la Mzimba, anthuwo adadabwa chimodzi mwa zimbudzi za pamalowa chikutulutsa fungo lodabwitsa. Malo ake ndi awa: Mmodzi mwa anthu okhala ku Hilltop kusonyeza dzenje la chimbudzi chomwe mudatayidwa khandalo Fungoli linatidabwitsa ndipo pokumbukira kuti Chonga adali ndi pathupi pomwe panasowa, tinadziwitsa a mfumu kuti afufuze, adatero mmodzi mwa anthuwo. Iwo adati mphekesera zili ponseponse kuti mayiyo adakangana ndi mwamuna wake yemwe amachita bizinesi ya kabaza. Akuti mwamuna wake amati pathupipo si pake ndipo mkaziyo azipita kwa mwini pathupipo, iwo adatero. Mkazi wa mfumu Chikundura ya deralo adati amayi anayamba kumudabwa mnzawoyo ataona kuti pathupi pomwe adali napo pasowa koma alibe khanda. Titamuona kuti alibe pathupi tili kumadzi, tidadabwa ndi kumufunsa komwe wasiya khanda lake, koma iye adakanitsitsa kuti adalibe pathupi, kunali kunenepa chabe, adatero mayi Chikundura. Iye adati apo ndi pomwe adadziwitsa akuluakulu kuti mnzawoyo wataya khanda. Ndipo nawo apolisi a mumzindawu atsimikiza kuti akusunga mchitolokosi Chonga, wa zaka 28, pomuganizira kuti adataya mwana mchimbudzi. Malinga ndi mneneri wa polisi ya Mzuzu, Martin Bwanali, Chonga, yemwe ali ndi ana asanu ndi mmodzi, komanso wina wakubere wa chaka ndi miyezi 7, adauza apolisi kuti adagwetsera chinthu mchimbudzimo atapita kokadzithandiza. Bwanali adati Chonga aonekera kubwalo la milandu masiku akubwerawa kukayankha mlandu wobisa pathupi. Iye adati mayiyo adamutengera kuchipatala cha Mzuzu Central kuti akamuyeze ngatidi adali ndi pathupi koma zotsatira zidali zisadadziwike pomwe tinkasindikiza nkhaniyi. ",7 " Ife toto takana! Mkozemkoze adanyula maliro aeni. Sinodi ya Livingstonia yatemetsa nkhwangwa pamwala kuti sipepesa monga momwe mafumu ena mboma la Rumphi alamulira. Pempho la mafumuwo likudza potsatira chipwirikiti chomwe chidachitika Lachiwiri msabatayi poyika mmanda thupi la malemu Chikulamayembe mbomalo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Nyondo akulankhula uku mafumu akukambirana zochita Sinodiyo idakolana ndi mafumu pa maliro a Chikulamayembe pamene idalamula kuti atsogoleri ena monga wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Saulos Chilima ndi mtsogoleri wa zipani zotsutsa, Lazarus Chakwera alankhulepo pa malirowo. Ukali wa mafumuwo udaoneka pamene adakalanda mkuzamawu kuti mlembi wa sinodiyo Levi Nyondo asalankhulenso. Nyondo sadanjenjemere koma kuwauza mafumuwo kuti ayendetse mwambo wa mapemphero zomwe zidakakamiza mafumuwo kupepesa kuti mwambowo uchitike. Izi ndizomwe zakwiyitsa mafumuwo motsogozedwa ndi mwana wa Chikulamayembe, Mtima Gondwe yemwe wati sinodiyo idanyazitsa maliro a bambo ake. Nchifukwa chake tikupempha kuti sinodi ipepese pa zomwe zidachitikazo. Dziwani kuti adamwalirawo adali bambo anga, ndiye ine komanso akubanja tidakhumudwa nazo, adatero Gondwe. Naye gulupu Kawazamawe yemwe amalankhuliranso banja loferedwa adati mafumuwo ali ndi mfundo zitatu. Kusalemekeza maliro a mfumu. Kuyambitsa chipwirikiti pamaso pa mtsogoleri wa dziko lino komanso kunena kuti Chilima ndi Chakwera alankhule zomwe zikadayambitsa ndewu, adatero Kawazamawe. Koma izi sizikutekesa sinodiyo pamene yati ilibe nthawi yopepesa munthu pa zomwe zidachitikazo. Mmodzi mwa akuluakulu a mpingowo, mbusa Douglas Chipofya adati boma ndi mafumu ndiwo akuyenera kupepesa mpingo. Komanso paja mafumu adapepesa kale kusiwa kuja choncho nkhanizi zidatha basi, adatero Chipofya. Mawu a Chipofya adagwirizana ndi mawu a Nyondo amene adatsindika kuti mafumuwo ndi amene akuyenera kupepesa kumpingo. Kodi chichitike nchiyani pamene mpingowo wakana kupepesa? Gondwe adati aona chomwe achite koma sadanene chomwe angachite. Koma T/A Mwamlowe amene ali pansi pa Chikulamayembe adati pa mwambo wa Atumbuka, mfumu ikalankhula, palibenso amene amalankhula pamwamba pake. Naye T/A Mwamlowe adati kukadakhala kwabwino mbali zonse zikadadya khonde momwe ndondomeko ya mwambowo ikhalire. Bungwe lachikhalidwe la Mzimba Heritage Association (Mziha) lidati zikuoneka kuti anthu ena sadapitire kukalira Chikulamayembe. Mmodzi mwa atsogoleri a Mziha, Ndabazake Thole adati mwambo wakumudzi ulemu umaperekedwa kwa mafumu, ndipo ampingo amabwera nkumatonthoza anamfedwa. Naye DC wa boma la Rumphi Fred Movete adati nthawi zonse mfumu ya ndodo ikamwalira, ofesi yake imapanga ndondomeko yakayendetsedwe ka mwambo mogwirizana ndi a banja komanso unduna wa zamaboma angono. ",1 " Wa zaka 18 akaseweza zaka 18 Bwalo lamilandu mumzinda wa Mzuzu lagamula Mulolo Nkhata wa zaka 18 kukakhala kundende zaka 18 atamupeza wolakwa pamlandu wogonana ndi mwana wa zaka 6. Zidamveka mbwalolo kuti mnyamatayo ankagwira maganyu kunyumba kwa makolo a mwana ochitidwa chipongweyo ndipo kaamba ka kubwerabwera kwake pakhomopo adayamba kudziwana ndi yo. Nkhata ndi wochokera mmudzi mwa Chikwina T/A Nyalubanga mboma la Nkhata Bay. Mneneri wa polisi mumzinda wa Mzuzu Patrick Saulosi adati Nkhata adavomera kulakwa kwake pamlanduwo. Iye adati woimira boma pamlanduwu, sub-inspector Lyson Kachikondo, adapempha bwalo lamilandu kuti chigamulo chikhale chokhwima kaamba kakuti mlanduwu ndiwaukulu komanso zomwe wamudutsitsa mwanayo ndi chinthu chomwe sangadzaiwale moyo wake onse. Ogamula mlanduwu, Tedious Masoamphambe adavomereza zomwe adanena Kachikondo ndipo adati chigamulo chachikulu chithandiza kuchepetsa kuchuluka kwa milandu ya ntunduwu, adatero Saulosi. Izi zili choncho bambo wa zaka 47, Wilson Nyirenda, wa mboma la Nkhata Bay wagamulidwa kukhala ku ndende zaka 14 atagonana ndi mwana wa zaka 12. Mneneri wa polisi wa mboma la Nkhata Bay Ignatius Esau adati mwezi wa August, Nyirenda yemwe ndi wochokera mmudzi mwa Chikalanda T/A Chikulamayembe ku Rumphi adamuitanira mwanayo mu nyumba mwake momwe adamugwiririra. Mwanayo adatuluka mnyumbamo akulira zomwe zidachititsa anthu kuti amufunse zomwe zamuchitikira ndipo mwanayo adaulula, adatero Esau. Iye adati Nyirenda adakana mulanduwo koma adapezeka wolakwa anthu anayi atachitira umboni za nkhaniyi. Iye adati anthu ankamunamizira chifukwa amachita naye nsanje poti siochokera mmudzimo. Adauzanso bwalolo kuti adali ndi matenda a chinzonono ndipo adauza makolo a mwanayo kuti apite naye kuchipatala. Adapitiriza kuti adakhala nthawi yaitali asadagonane ndi mkazi ndipo ngati adagwiririradi mwanayo ndiye kuti adampatsa mimba, adatero Esau. Iye adati ogamula mlanduwu, Billy Ngosi, adati milandu yogwiririra ikukula ndipo olakwa akuyenera kupatsidwa chigamulo chonkhwima kuti chikhale chiletso kwa ena. ",7 "Amayi Ali Ndikuthekera Kothana Ndi Kusintha Kwa Nyengo-CADECOM Bungwe loona za chitukuko mu mpingo wakatolika la CADECOM mu dayosizi ya MANGOCHI lati amayi ali ndi udindo pa ntchito yothana ndi vuto la kusitha kwa nyengo komanso kuonongeka kwa nthaka. Mlangizi wamkulu wa bungweli a PETER NTHENDA ndi yemwe wanena izi polankhula ndi mtolankhani wathu yemwe amafuna kudziwa momwe kusintha kwa nyengo kumakhudzira amayi mu dayosiziyo. A NTHENDA ati amayi ndi ndi amene amatenga gawo lalikulu mu ntchito zosiyanasiyana mdziko monga , ulimi , komanso ntchito zapakhomo , choncho ali ndi kuthekera kothana ndi vuto lakusintha kwa nyengo , komanso kubwezeretsa nthaka pochita ulimi wa kasakaniza. Tikanena zakusintha kwa nyengo ku malawi kuno zinthu zimene zimayambitsa ndi ulimi komanso zankhalango, tiona kuti amayi ndiwo amatenga gawo lalikulu pa ulimi kuno ku malawi chachiwiri nchoti amayi ndiwo amatanganidwa kukonza chokudya pakhomo zomwe zimafuna khuni zambiri ndiye tikuwapempha azimayi kuti azigwiritsa mbaula zosalirana nkhuni zambiri komanso tikuwapempha azimayi kuti azigwiritsa ma basiketi a sungu kapena amulaza osati ma pulasiti komanso kubvala mitengo pofuna kubwezeretsa thaka anatero a Nthenda. Polankhulapo mayi VIOLET KANDULU kuchokera ku Arch dayosizi ya BLANTRYE ati amayi kuti sakuyenera kutaya zinthu zomwe zimaononga nthaka mwachisawawa ndi cholinga chakuti ayiteteze. Atiphunzintsa manphunziro akulu monga azimayi timataya zinyalala mmakwalala mwathu moma kutaya ma pampa komanso ma pulasitic zomwe zikupangitsa kuti nthaka yathu iwonongeke. Choncho tikhale oyamba kuchotsa zinyalala zomwe zimaonnga chilengedwe pakutero anthu azaphunzirira kwa ife anatero mayi Kalundu. ",18 "Kabwira Alimbikitsa Sukulu za Mkomba Phala Wolemba: Glory Kondowe nt/uploads/2019/10/Kabwira.jpg"" alt="""" width=""201"" height=""250"" />Kabwira: Tiona momwe zithere Dr. Jessie Kabwira ati kulimbikitsa ntchito za sukulu za mkomba phala komanso kuika chidwi pa ndondomekoyi kungathandize kutukula maphunziro mdziko muno. Dr. Kabwira omwe anali phungu wa kunyumba ya malamulo mdera la kumpoto chakuzambwe kwa boma la Salima ati ngakhale sanachite bwino pa zisankho zomwe zinachitika mdziko muno mmwezi wa May chaka chino, ngati mzika yokonda dziko lake, akuyenera kuthandizirapo kuti zinthu zina zidziyenda bwino. Iwo ati dziko kuti litukuke pakuyenera kukhala ndondomeko zabwino kuti anthu adzikhala ndi chakudya komanso madzi a ukhondo. Zili kwa iwowo anthu kusiyanitsa ntchito zomwe ndagwira kwa zaka 5 ndi wina amene amusankhayo. Anthu a mboma la Salima kumpoto chakumadzuro ndi mboni yanga ikakhala nkhani ya madzi, malo komanso chakudya pakadali pano akudziwa Mulungu. Tiona kuti zitha bwanji, anatero Dr. Kabwila. Iwo ati zomwe zimawakhuza kwambiri ndi khani ya njala ndipo apemphanso kuti chitukuko cha sukulu, madzi ndi chakudya chipite patsogolo mderalo. ",3 " Ku Nkhoma sakugona ndi mthirira Amati mmera mpoyamba. Ukalephera kukonzekera koyambirira ntchito yonse imayenda mwapendapenda mpaka zipatso zake zimakhala zokhumudwitsa. Ino ndi nyengo ya dzinja ndipo ulimi wagundika ndi wamvula, koma alimi ochangamuka pano ayamba kale kukonzekera za mthirira wachilimwe chomwe chikubwera kutsogoloku. Ena mwa alimi omwe akuonetsa chitsanzo chabwino pakukonzekera mthirira wamtsogolo ndi a ku Nkhoma mboma la Lilongwe. STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi wapampando wa gulu la alimiwa, Lingilirani Chikhwaya pazomwe akuchita, motere: Chikhwaya: Sitivutika kumbali ya chakudya Ndikudziweni wawa Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ine ndine Lingilirani Chikhwaya ndipo ndine wapampando wa alimi a mthirira omwe amathandizidwa ndi bungwe la Vision Fund Malawi kudzera mthumba la ngongole za ulimi la Mthirira Loans. Mulipo alimi angati? Tonse tilipo alimi 222 omwe timathandizidwa ndi Vision Fund Malawi koma aliyense ali ndi munda wakewake momwe amalima mbewu yomwe iye akuona kuti imuchitira bwino ndipo apindula nayo. Ndi mbewu zanji zomwe zimalimidwa kwambiri? Ambiri amalima chimanga, nyemba, tomato, anyezi ndi ndiwo zamasamba zosiyanasiyana. Ambiri mwa ife timakonda kasakaniza monga kubzala chimanga limodzi ndi nyemba kapena kugawa kuti mbali ina tomato, ina anyezi ndipo ina masamba monga chomoliya, mpiru kapena kabichi. Ulimi umenewu ukukupindulirani bwanji? Ulimiwu tikupindula nawo kwambiri chifukwa usadabwere, ambirife tinkavutika kwambiri kupeza zipangizo zaulimi dzinja likafika kusowa pogwira, koma pano zinthu zidasintha. Tikamachita mthirira wathu timakhala tikusunga pangonopangono ndalama mwinanso nkumaguliratu zipangizo zaulimi nkumasunga. Tikatero, dzinja ngati lino likafika timakhala tilibe nkhawa. Kupatula apo, sitivutika kumbali ya chakudya chifukwa timati tikamadya zamvula, zamthirira zikucha kuti zamvulazo zikamadzatha, tidzayambe kudya zamthirira. Mukuoneka kuti muli kalikiriki mmunda wa mthirira pomwe lino ndi dzinja simukupotoza pamenepa? Ayi ndithu, umu ndimo timachitira. Kuteroku tayambiratu kukonzekera mthirira wachilimwe chikubwerachi. Pali zambiri zomwe timayenera kupangiratu monga kusunga madzi okwanira, kuteteza maiwe anthu kuti asadzadze komanso kutchingira mmalo momwe mumathamanga madzi kuti asaononge nthaka. Kungolekerera nthaka imakokoloka ndiye poti munthu udzayambe kulima ulimi wamthirira zofuna zimachuluka monga kusonkhanitsa manyowa obwezeretsera nthaka yomwe idakokolokayo. Panopa yakula ndi ntchito iti? Monga ndanena kale, pakalipano ntchito yaikulu ndi yosunga madzi. Ulimi wathu wamthirira timadalira msinje ndiye chaka ndi chaka ngati panopa timatchingira kuti madzi asathawe. Timapanganso mizere ikuluikulu yotchinga madzi kuti azilowa pansi kuti mvula ikadzatha, pansi padzakhale chinyezi kwathawi yaitali tisadayambe kuthirira. Tafotokozankoni nkhani ya misika, mumagulitsa kuti zokolola zanu? Ambiri mwa ife timadalira kugulitsa kumisika ndi kupikulitsa kwa anthu omwe amakagulitsa kumsika. Si misika yodalirika, ayi, komabe timapezamo kangachepe. Pakalipano omwe amatithandiza ndi ndalama za ngongole a Vision Fund Malawi akutithandiza kuyangana misika yodalirika moti posachedwapa tikhala tikusimba lokoma. Mudalingalirako zopanga magulu ogulitsira katundu wanu pamodzi? Maganizo amenewo ndiwo tikupanga tsopano nchifukwa chake tili kalikiriki kusakasaka misika yokhazikika komanso paja ndati pakalipano mlimi aliyense ali ndi ufulu wolima mbewu yakukhosi kwake ndiye tikufuna kuti tikapeza msika wokhazikika, tizidziwa mbewu zoyenera kulima. Nanga si msika wapezeka kale? Kaya tsogolo la ulimi wanu mukuliona bwanji? Tsogolo ndi lowala kwabasi chifukwa momwe tidayambira ndi pomwe tili pano zikusiyana kwambiri. Mbewu zomwe tinkakolola kale ndi zomwe timakolola pano zimasiyana kwambiri chifukwa pano tidapatsidwa upangiri wapamwamba ndi alangizi odziwa ntchito yawo. Chiyembekezo chathu nchakuti mzaka zikudzazi tizidzalima ndi kukolola mbeu zoti mwinanso nkumadyetsa chiwerengero cha anthu ochuluka chifukwa, mwachitsanzo, chaka chino tathandiza anthu ambiri ndi chimanga chomwe tidalima kusikimu ndipo nafenso tapeza phindu lochuluka kwambiri. Malangizo anu ndi otani kwa alimi anzanu? Malangizo anga ndi oti alimi asamakonde kukhala pansi ayi. Ntchito yathuyi imasiyana kwambiri ndi ntchito zina chifukwa ife ndiye timadyetsa mtundu wonse. Tizionetsetsa kuti mvula ikamapita kumapeto, ntchito ya kusikimu yayamba ndipo chilimwe chikamapita kumapeto, tizionetsetsa kuti tayambiratu kukonzekera ulimi wa mthirira wotsatirawo ngati momwe tikuchitira ifemu. Izi tikuchita apazi ndi chiyambi chabwino chifukwa sitidzakhala ndi ntchito yambiri mthirira ukamadzayamba. ",4 "Ofesi ya Zaumoyo ku Blantyre Yati Ilimbikitsa Chitetezo cha Antchito Ake Ofesi yowona zaumoyo mu mzinda wa Blantyre yati ndi yokonzeka kulimbana ndi kachilombo ka Coronavirus popereka zipangizo zokwanira, zozitetezera ku matendawa kwa omwe akugwira nchito zachipatala mu mzindamo. Kawalazira: Tiyenera kuteteza miyoyo ya ogwira ntchito zachipatala Malingana ndi Mkulu wa zaumoyo mu mzinda-wu, Dr. Gift Kawalazira, ofesiyi yakhazikitsa njira zabwino pofuna kuteteza anthu ogwira ntchito zachipatala omwe akuthandiza anthu omwe akhuzidwa ndi nthenda ya COVID-19. Iwo ati chipatala cha Queen Elizabeth ndi komwe anthu azachipatala azithandizidwa ngati akhudzidwa ndi nthendayi pomwe anthu ena onse azikasamalidwa ku chipatala cha Kameza mu mzinda omwewo wa Blantyre. Choyamba tiyenera kuteteza miyoyo ya ogwira ntchito zachipatala mu mzinda wa Blantyre kuti atumikire moyenera choncho chipatala cha Queen Elizabeth Central ndi chomwe chizithandiza anthuwa, ndipo anthu ena onse okhala mu mzindawu azithandizidwa kwa Kameza komwe kuli sukulu ya anamwino ya Kamuzu College of Nursing, anatero a Kawalazira. Pamenepa Dr. Kawalazira anati chiwerengero cha odwala matendawa chikamachuluka akafikira msukulu zosiyana siyana ndi cholinga chopeza malo okwanira osamalira odwalawa. ",6 " Nkhanza zapolisi zanyanya Ophunzira 24 a kusukulu za ukachenjede apereka maina awo ku bungwe la maloya la Malawi Law Society (MLS) za nkhanza zimene achitiridwa panthawi yomwe amachita zionetsero zokwiya ndi kukwera mtengo kwa fizi. Iwo adachita izi MLS itawapempha kuti apereke mainawo potsatira nkhanza zimene apolisi adachitira ophunzirawo amene akwiya kuti fizi zakwera kuchokera pa K275 000 kufika pa K400 000. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Apolisi kuponda mwana akufuna kutolera mabotolo ku Kamuzu Stadium Nkhanzazo zidafika pambalambanda kwambiri ena atajambula pa vidiyo wapolisi wina ataomba khofi wophunzira wa chaka cha chinayi Mayankho Kapito, yemwe ndi mwana wa mkulu wa bungwe loona zaufulu wa anthu ogula la Consumers Association of Malawi (Cama) John Kapito. Kapito wati asumira apolisiwo. Mtsogoleri wa ophunzira ku Chancellor College Ayuba James adatsimikiza kuti pofika Lachitatu chiwerengero cha ophunzira omwe adapereka maina awo adali atafika pa 24. Talandiradi mainawo koma tikudziwa kuti chiwerengero chayenera kukhala chokwera kwambiri chifukwa ambiri apitapita mmakwawo. Nkovuta kuti uthengawu uwafikire, adatero James. Chikalata cha MLS chidapempha ophunzira amene angakhale ndi umboni wa nkhanzazo kuti apereke maina awo. Ngakhale mneneri wa bungwelo Khumbo Soko adatsimikiza za ntchitoyo, adakana kuthirirapo ndemanga chifukwa ati akadali mkati mopeza mainawo. Nthawi ya zionetsero za ophunzirawo, apolisi akhala akumenya ophunzirawo ndipo amangapo angapo pa zipolowe zomwe zakhala zikuchitika msukulu zomwe zili pansi pa University of Malawi (Unima). Izi zili apo, mabungwe ena a zaufulu wa Amalawi ati nkhanza zankitsa kupolisi ndipo ati izi zikusemphana ndi zimene amalengeza kuti adasintha. Sabata yatha, dotolo wodziwika bwino Dr Frank Taulo adalemba pa Facebook kuti adapeza apolisi akumenya anthu amene adawapeza akungoyenda mu Limbe mumzinda wa Blantyre nthawi itangokwana 6 koloko madzulo. Nditawafunsa chifukwa chiyani amamenyera anthuwo, adandikuta. Nditawauza kuti ndine wakuti, sadalabadire ndipo adandionongeranso galimoto langa, adatero Taulo. Posakhalitsapa, mwini malo ena a chisangalalo ku Chigumula mumzindawu, Sharat Gondwe adatinso apolisi adamumenya atabwera kudzatseka malo akewo, Pitchers Club. Anthu ena amene tidacheza nawo ku Lilongwe nawo adasimba za nkhanza za apolisi. Gift Potani wa kumsika wa ku Area 24, Andrew Mwenye wa mumsika wa Tsoka komanso Alinafe Matthias wa ku Area 22 adanena kuti apolisi akumanga anthu kapena kuwakwapula kumene opanda chifukwa chenicheni. Nthawi zina amapeza anthu malo omwera masanasana nkuwaphaphalitsa, ena kutengedwa osapatsidwa mpata wofotokoza zomwe akuchita, adatero Potani. Si ana a sukulu kapena Amalawi wamba amene akudandaula za nkhanzazi. Nawo amayi oyendayenda ati amakumana ndi nkhanza za apolisi akagwidwa pantchito yawoyi. Mneneri wa bungwe loyimilira amaiwa, Zinenani Majawa, adati pakati pa apolisi pali Chichewa choti Dzipulumutse kutanthauza kuti wogwidwayo apereke kena kake kapena akakhala mzimai asinthitse thupi lake ndi ufulu. Apolisi akatigwira vakabu amati dzipulumutse wekha kutanthauza kuti akufuna ndalama ndipo ngati palibe amamumenya kapena kumugona mzimai popanda chitetezo chilichonse ndiye poti ndi wapolisi, kokanena kumasowa, adatero Majawa. Mkulu wa bungwe la zaufulu la Centre for Human Rights and Rehabilitation (CHRR) Timothy Mtambo adati apolisi akadaunika mofatsa magwiridwe awo antchito kuti pomwe akuteteza miyoyo ndi katundu, asamaphwanye ufulu wa ena. Mneneri wa apolisi mdziko muno Nicholas Gondwa adaikira kumbuyo apolisi ndipo adati akugwira ntchito yawo potsata malamulo. Mawuwo adadza pomwe apolisi adalengezanso kuti akufufuza za wapolisi wothyapa khofi mwana wasukulu. Tikafika poponya utsi okhetsa misozi ndiye kuti zionetsero zafika pa zipolowe pofuna kuteteza anthu amene sizikuwakhudza ndi katundu wawo. Komanso kumanga ena mwa anthuwo kumakhala kuziziritsa zipolowezo, adatero Gondwa. ",7 " Zili bwinoPAC Nduna yakale ya zaulimi George Chaponda yamangidwa patatha masiku 43 kuchokera pamene nthumwi kumsonkhano wa Public Affairs Committee (PAC) lidapatsa boma masiku 30 kuti limange ndi kuzenga mlandu ndunayo poyiganizira kuti idachita zachinyengo. Imodzi mwa mfundo zimene nthumwizo zidamanga pamsonkhano umene udachitika mumzinda wa Blantyre pa 7 ndi 8 June, idali yoti Chaponda amangidwe malinga ndi kafukukufuku amene makomiti a Nyumba ya Malamulo adachita ndi kupeza kuti ndunayo idachita za chinyengo pogula chimanga ku Zambia. Komiti ina imene adakhazikitsa mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika idapezanso kuti Chaponda adachita ukapsala. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Chaponda (Kumanja) ndi Tayub kufika kukhoti Lachinayi Bungwe la ACB Lachitatu lidamanga Chaponda limodzi ndi mkulu wa kampani ya Transglobe Rashid Tayub komanso wapampando wa bungwe loona za malonda a mbewu zosiyanasiyana la Grain Traders Association of Malawi, Grace Mijiga Mhango. Lachinayi, oyimira Chaponda adapempha bwalo la majisitileti kuti lichotse chikalata choti mkuluyo amangidwe koma bwalolo lidakana pempholo choncho adagonanso mchitokosi. Mhango adapatsidwa belo Lachitatu. Ndipo madzulo a tsiku lomwelo, bwalolo lidapereka belo kwa Chaponda ndi Tayub. Mneneri wa PAC Peter Mulomole adati akuyembekezera kuti ACB ipitiriza ntchito imene ayiyambayi mpaka kumapeto kuti chilungamo chidziwike. Uku ndiko kukhala. Aliyense aziyesedwa ndi mlingo umodzi chifukwa palibe yemwe ali pamwamba pa malamulo. Chiyembekezo chathu tsopano nchoti momwe zateremu, ACB ikoka nkhaniyi mpaka kumapeto, adatero Mulomole. Mkulu wa bungwe la Centre for the Development of People (Cedep), Gift Trapence, wati zomwe yachita ACB zaonetsa kuti bungweli layamba kugwira ntchito mosaopsezedwa. Uku ndiye timati kukula. Bungwe la ACB siliyenera kugwira ntchito mwamantha kuopa maina. Apa tikuyembekezera kuti zonse ziyenda bwino mpaka chilungamo chioneke, adatero Trapence. Mwezi wathawu, Chaponda adanena poyera kuti iye ndi wokonzeka kunjatidwa ngati Amalawi akuona kuti ndiwolakwa koma iye adabwereza kuti akudziwa kuti akufera kuthandiza Amalawi omwe akadafa ndi njala. ",11 " Anatchezera Wamboni, ine Msilamu Zikomo Anatchereza, Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Ndinagwa mchikondi ndi mtsikana wa Mboni za Yehova mpaka ndinamuchimwitsa moti ndikunena pano kuli mwana wamphongo. Makolo ake atamufunsa ananditchula ineyo ndipo atandiitana ndi akwathu ndidavomera mlanduwo. Makolo a mtsikanayu adati ngati ndikufuna kuti zithe bwino ndilowe mpingo wawo kuti asakandisumire kukhoti komanso kuti ndizisamalira mwana wangayo. Ine sindikufuna kulowa mpingowo, koma mtsikanayu akuti akhoza kulola kulowa Chisilamu ngati makolo ake angalole. Kodi apapa ndiye nditani kuti mwanayu ndizimusamalira popanda kulowa mumpingo wawowo? Kodi nditani kuti mkaziyu ndimukwatire? BJ, Lilongwe BJ, Mwazingwadi, achimwene a BJ. Vuto lili apa ndi loti inuyo simufuna kulolera zofuna za makolo a mkazi munamuchimwitsayo koma mukufuna zanu ziyende basi! Sizikhala choncho mukafuna kulowa moyo wa banja. Kulolerana ndiye gwero la banja. Mkazi munamuchimwitsayo waonetsa kale chikondi chake kwa inu chifukwa akulolera kuti atha kukutsatirani ku Chisilamu bola makolo ake amulole, koma inu chikondi chanu nchoperewerako pangono chifukwa mukumenyetsa nkhwanga pamwala kuti simungayerekeze kulowa mpingo wa mkazi wanuyo. Mulungu ndi mmodzi, baba, mipingo ndiye njambirimbiri! Langizo langa apa ndi loti zonse zimatha nkukambirana. Ngati akuchikazi nawonso sakulolera zoti mwana wawoyo alowe Chisilamu, monga inuyo mmene mwakanira kuti simungalowe mpingo wa Mboni za Yehova, kwatsala njira imodzimuthabe kulowa mbanja, koma aliyense akhale ndi ufulu wokapemphera koma akufuna. Zikakaniza apo, ndiy kaya. Ndakhala ndikunena nthawi zambiri kuti banja si masewera; pamakhala zambiri zofuna kutsatidwa musanalowane, koma mukadya mfulumiza, mavuto ake amakhala ngati amenewa. Koma, baba, nzoona mungalephere kuthandiza mwana wanu kaamba ka kusiyana mipingo? Mwana adalakwa chiyani? Nzoona makolo a mkazi akukuletsani kuthandiza mwana wanu kaamba koti simunalowe mpingo wawo? Chonde, mwana yekhayo asavutike chifukwa cha nkhani yanu. Muzimuthandiza mjira iliyonse, makolo a mkazi ndikhulupirira sadzaona cholakwika mwana wanu akamalandira thandizo kuchokera kwa bambo ake omubereka. Amandikakamiza zogonana Agogo, Ndine mtsikana wa za 17 ndipo ndili ndi chibwenzi chomwe chimandikakamiza kuti tiyambe kugonana. Nditani? Mwana wanga, musiye ameneyo, sadzakuthandiza! Ndipo wachita bwino kundiuza msanga za nkhawa yako. Anzako ambiri amakopeka ndi zautsiru ngati zimene akukukakamiza bwenzi lakolo ndipo mapeto ake ndi kutengapo mimba kapena matenda opatsirana pogonana. Anyamata kapena abambo ambiri si okonzeka kuvomereza kuti ndiwo akupatsa pathupi kapena matenda ndiye chimakutsalira, tsogolo lako nkupiratu pamenepo. Fatsa, mwana wanga, sunga khosi ndipo mkanda woyera udzavala! Ukadzisunga udzaona kukoma moyo wako onse utapeza mwamuna weniweni amene adzakukonde ndi mtima wake wonse, osati kamberembere amene akuti muzigonana panopa muli pachibwenzi. Umuuziretu kuti iwe si chidole choseweretsa. Asaa! Ofuna mabanja Ndikufuna mkazi wa zaka 19-23 komanso woopa Mulungu0881 131 533 Ndine mkazi wa zaka 33 ndipo ndili ndi mwana mmodzi. Ndili ndi kachilombo ka HIV koma ndikumwa mankhwala. Ndikufuna mwamuna wa zaka 35-37. Wondifuna aimbe pa 0882 617 531 Ndine mwamuna wa zaka 35 ndipo ndi ana awiri. Ndikufuna wachikondi woti ndikwatire, akhale Mkhristu wa zaka 25-30 wokhala ku Lilongwe konkuno. Akhale wokonzeka kukayezetsa magazi. Wondifuna andiimbire pa 0882 511 934. ",12 " Amalawi apindulanji ndi kutsogolera Sadc Doko la Nsanje: Kodi liona kuwala tsopano? Akuluakulu pa zachuma komanso mafumu mdziko muno ati mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda afunika masomphenya kuti dziko lino lipindule pamene ali wapampando wa mgwirizano wa maiko a kumwera kwa Africa wa Southern Africa Development Community (Sadc). Banda wangosankhidwa sabata yathayi pamsonkhano wa Sadc omwe umachitikira ku Lilongwe komwe atsogoleri a maiko 14 adasonkhana. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Aka sikoyamba mtsogoleri wa dziko la Malawi kusenza udindo wotsogolera mabungwe a maiko angapo. Mtsogoleri wakale Bakili Muluzi adalinso mtsogoleri wa Sadc. Ndipo mnthawi yaulamuliro wake, Bingu wa Mutharika adali wapampando wa African Union (AU). Koma monga akunenera nduna yakale ya zachuma Friday Jumbe komanso kamuna pa zachuma ku bungwe la Malawi Equity Justice Network (MEJN) Dalitso Kubalasa, Banda akuyenera akhale ndi masomphenya ngati akufuna kuti dziko lino lipindule panthawiyi. Utsogoleri wa Banda ukudza pamene boma lake lili kalikiliki kukozanso chuma cha dziko lino kuti Amalawi ayambe kusimba lokoma. Panthawiyi ali ndi mphamvu yokwaniritsa zomwe amalakalaka zitachitika mdziko muno. Chitsanzo mtsogoleriyu wakhala akukamba za malonda a dziko lino ndi maiko ena zomwe zingatheke nthawiyi. Chikufunika ndi kukhala ndi masophenya chifukwa mphamvu zonse ndiye zili mmanja mwake komanso kuti Economic Recovery Plan itheke nthawi yake ndi imeneyi, adatero Kubalasa. Mfumu yayikulu Kwataine ya ku Ntcheu yati uwu ndi mwayi kuti nkhani za uchembere wabwino zipite patsogolo mdziko muno ndi maiko ena. Nkhani za uchembere wabwino komanso ulimi zikufunikira ukadaulo, kukaphunzira momwe anzathu amachitira mmaiko akunjawo. Pamene apulezidentiwa ali mtsogoleri wa Sadc tikukhulupirira kuti zinthu zimenezi tipita chitsogolo komanso nduna zawo zizikhudzidwa ndi nkhanizi, adatero Kwataine yemwe adayamikira mapulani a mtsogoleriyu. Naye Malemia wa ku Nsanje wati kumeneko adayandikana ndi dziko la Mozambique zomwe wati zithandiza maka kumbali ya ubale. Asodzi a ku Mozambique amabwera ku Malawi komanso ife timapita mzipatala za dziko lawo. Izi kuti zidzichitika zimafunika ubale wabwino pakati pa mayiko awiriwa.Tikukhulupirira kuti izi zilimbikitsa ubale wathu, adatero Malemia. Jumbe wati Banda ali ndi mwayi kuti wakhala mtsogoleri pamene dziko lino likukumana ndi mavuto achuma komanso mikangano ya nyanja ndi dziko la Tanzania zomwe wati zingatheke ngati atagwiritsa bwino nthawiyi. Mkangano wa nyanja ungakambidwe bwino pamene akutsogolera Sadc. Komanso amakamba za zokopa alendo zomwe zingathandize nkhani zachuma. Pakufunika kuti panthawiyi misonkhano ikuluikulu izichitika ku Malawi kuno kuti nkhani zokopa alendo zipite patsogolo, komanso pakufunika kuti akhazikitse mgwirizano wabwino wa dziko lino ndi maiko omwe ali mu Sadc kuti zamalonda zipite patsogolo monga iye mkhalapampando, adatero Jumbe. Poyangana mmbuyo pamene Muluzi adali wapampando wa Sadc, Jumbe wati panthawiyo dziko lino lidapindula pankhani ya ubale wa dziko lino ndi maiko ena. Ngati ubale wa maiko uli bwino, malonda amayenda bwino komanso anthu amalowa ndi kutuluka mdzikomo momasuka popanda chiopsezo, adatero Jumbe. Banda yemwe wachiwiri wake ndi mtsogoleri wa dziko la Zimbabwe Robert Mugabe watenga udindowu kuchokera kwa mtsogoleri wa dziko la Mozambique Armando Emilio Guebuza. Kusankhidwa kwa atsogoleriwa akuti kumachitika malinga ndi zomwe ofesi ya Sadc imagwirizana. Amawafunsa pambali ngati angakhale mtsogoleri wa Sadc, akavomera ndi pamene amadzasankhidwa kuti akhale mtsogoleri. Maiko osauka ambiri ndiwo amatengeka ndi utsogoleriwu koma maiko ochita bwino monga South Africa satengeka nazo. Mungaone kuti Muluzi adakhalapo, pano Joyce Banda wangolowa kumene koma lero tikukamba kuti ndi mtsogoleri wa Sadc, adatero Jumbe. Mdziko muno muli mapulojekiti omwe atatha angathandize Amalawi monga doko la Nsanje. Ntchito pa dokoli zidayima chifukwa chosagwirizana zingapo ndi dziko la Mozambique. Angoni alirira mafumu GEORGE SINGINI Angoni a ku Mzimba ati kumwalira kwa mfumu yawo yaikulu kwambiri Inkosi ya Makosi Mmbelwa ndi mfumu yaikulu Jalavikuwa chaka chino kudzetsa mavuto pankhani ya ulamiro pakati pa Angoni. Inkosi Mmbelwa adamwalira mu February pamene Jalavikuwa adamwalira sabata yathayi. Mafumuwa ndi omwe adali aakulu mu zaka ndipo kumwalira kwawo kwapangitsa kuti ulamuliro wa Chingoni ukhale mwa achinyamata. Inkosi Mabulabo yemwe ndi mfumu yachinyamata wati mtundu wachingoni wasokonekera mmaganizo ndi imfa za mafumu awiriwa omwe amwalira motsogozana. Mabulabo adati mafumu awiriwa adali ofunika paulamuliro wa Chingoni chifukwa adali okhwima nzeru ndi maganizo. Mfumuyo idati poti kwangotsala achinyamata zikhala zovuta paulamuliro wa chingoni. Pano sitikudziwa kuti atisogolere ndani. Tataya atsogoleri ofunikira kwambiri. Atsogoleri otha kuyanjanisa anthu, opemphera komaso odzichepesa, adatero Mabulabo. Mfumu ina ya Chingoni, Inkosi Mpherembe adati atha nzeru ndi imfa za mafumu awiriwa ndipo adati Jalavikuwa adali mgodi wa chikhalidwe cha Chingoni ndipo akanathandiza kwambiri kuyanjanitsa Angoni ndi mmene anamwalira a Mbelwa. Timalira kufa kwa Inkosi ya Makosi Mmbelwa yomwe inali mfumu yathu yaikulu. Ndi kumwalira kwawo timadalira a Inkosi Jalvikuwa kuti ndi omwe azitithandiza pa ulamuliro. Iwo anali ofunikira kwambiri popereka uphungu komanso kuyanjaniza anthu, adatero Mpherembe. Iye adati kuti zinthu zisasokenekere kwambiri akhala okakamizidwa kusaka anthu achikulire a chingoni kuti aziwathandiza mmaganizo. Koma anthuwa sangawafaninze ndi mmene akanachitira mafumu. Mlembi wa mkulu wa CCAP Synod of Livingstonia mbusa Levi Nyondo wati Angoni ali pamavuto aakulu ndipo monga mpingo awaika mmapemphero kuti zinthu zikhale mchimake. Bwanamkubwa wa Mzimba mbusa Moses Chimphepo wati kupita kwa mafumuwa kusokonezaso ntchito zaboma kamba koti anali olimbikira pachitukuko. Wachiwiri kwa nduna ya maboma angno ndi chitukuko cha mmidzi a Godfrey Kamanya agwirizana nazo kuti angoni ali pa mavuto aakulu chifukwa ataya odziwa chikhalidwe. ",10 "Akagwira Jere Zaka Zinayi Kaamba Kobaya Mlamu Wake Bwalo la Mangochi First Grade Magistrate lalamula bambo wina wa zaka 28 kuti akakhale ku ndende kwa zaka zinayi kaamba kobaya ndi kuvulaza mlamu wake. Bwaloli linamva kuchokera kwa woyimira boma pa mlandu, Sub Inspector Regina Makwinja kuti mkuluyu Joseph Kamanga anabaya mlamu wake Prisca pa nthawi yomwe amateteza mchemwali wake Mwandida pomwe amamenyedwa ndi mamuna wakeyu. Makwinja anati pa 11 March 2020, Joseph amamwa mowa pa malo ena pa msika pa Mpondasi mbomalo ndipo mkazi wake anafikanso pamalopo kudzapereka chakudya kwa mchemwali wake. Mkaziyu akuti anayamba kumwa mowa ndipo ataledzera anayamba kucheza ndi amuna ena omwe anali pamalopo zomwe zinakwiyitsa mamunayo ndi kuyamba kumumenya. Pamene Prisca adaganiza zolanditsa mchemwali wakeyo, ndi pamene Joseph adatenga galasi ndi kumubaya mlamu wakeyu pakhosi. Popereka chigamulo chake, First Grade Magistrate Roy Kakutu anati wapereka chilango cha mtunduwu kuti ena atengerepo phunziro. A Joseph Kamanga amachokera mmudzi mwa Mtalimanja mfumu yaikulu Mponda, mboma lomwelo la Mangochi. ",7 " Mswati adakali mfumuBoma Boma, kudzera mwa mneneri wa unduna wa maboma aangono ke Muhlabase Mughogho, lati ngakhale pali kukokanakokana pa ufumu wa Gomani V, boma likuvomerezabe Mswati Gomani wachisanu kuti ndiye mfumu. Mughogho adanena izi pamene mbali ina ya banja la Gomani motsogozedwa ndi Dingiswayo yalengeza kuti Dingiswayo ndiye mfumu, kulanda ufumuwu kwa Mswati. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Gomani V Lachiwiri akuluakulu ena abanja adatsutsa zomwe Dingiswayo adalengeza kuti Mswati adakalibe mfumu. Koma patangodutsa tsiku abanjawa atalankhula, Dingiswayo adachititsanso msonkhano wa atolankhani kuti zomwe adanena abanjawa ndizabodza ndipo iye ndiye mfumu yatsopano. Panopa ofesi ya Gomani yasamuka kuchoka ku Lizulu ndipo tikulankhulamu ili kwa Nkolimbo, adatero Dingiswayo. Koma malinga ndi Mughogho, Mswati ndiye mfumu. Boma likudziwa Mswati kuti ndiye mfumu, izi zili choncho chifukwa mfumu ikasankhidwa ndi abanja, boma limavomereza ndipo mwambo udachitika wodzoza Mswati kukhala Gomani wachisanu. Izi sizidasinthe mpaka lero. Gawo 11 (1) la malamulo okhudza mafumu, Chiefs Act la mchaka cha 2000 limati pulezidenti wa dziko ndiye ali ndi mphamvu yochotsa Paramount Chief, Senior Chief, Chief komanso Sub Chief. Mswati adadzozedwa mu pa August 10, 2012 kukhala Gomani wachisanu kutsatira imfa ya bambo ake. ",11 " Akudyerera obwela A malawi akhala akuingidwa ngati nkhuku mmaiko ena akafuna thandizo la chipatala, koma nzika zakunja kumadzawamwera mazira zikafika mdziko muno ponama kuti ndi nzika za dziko lino. Izitu zakhala zikuchitika chifukwa chosowa chiphaso cha unzika, koma lero mpumulo wafika kwa Amalawi pamene akhale ndi mwayi wokhala ndi chiphaso chosonyeza unzika wa dziko lino. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Kuthithikana mzipatala zina kumadza chifukwa cha anthu a kunja Zili chonchi malinga ndi ntchito yomwe bungwe la National Registration Bureau (NRB) poyamba kalembera wa unzika amene adayamba ndi akuluakulu aboma komanso maboma 11. Monga akufotokozera Senior Chief Kanduku wa mboma la Mwanza, boma lake limalandira nzika zambiri kuchokera mdziko la Mozambique. Anthu pafupifupi atatu mwa 10 alionse amene amafuna thandizo lachipatala kuno amakhala a ku Mozambique. Vuto ndiloti kuyambira pa Zobue mpaka ku Tete mdziko la Mozambique palibe chipatala, posowa kolowera, anthu adera limeneli amathandizidwa mzipatala za dziko la Malawi, adatero Kanduku. Ngakhale tayandikana ndi dzikolo, satilola kupita mdziko lawo kukalandira thandizo la chipatala. Amalawi angapo akhala akuthamangitsidwa, ndipo suthandizidwa chifukwa anzathuwo ali ndi zitupa za unzika, adaonjeza motero. Naye Senior Chief Kabunduli ya mboma la Nkhata Bay, adati kumeneko nzika za maiko a Tanzania zimalowa pafupifupi tsiku lililonse ndi kumalandira thandizo lomwe Amalawi amayenera kulandira. Akafika kuno amakhala ndi maina a Chimalawi zomwe ndizovuta kuwakaikira kuti si nzika zathu. Mankhwala pachipatala amatha mwachangu ife ndi kumavutika pamene iwo kwawo ali ndi zipatala zomwe zingawathandize, adatero Kabunduli. Kungofika pa Chintheche pali anthu ambiri amaiko a Burundi, sangapitenso kwawo ndipo akulandira chithandizo chilichonse chomwe chimayenera chipite kwa Amalawi. Kwawo sungayerekeze kupanga zimenezi koma ifeyo amationa kupusa, adaonjeza Kabunduli. Kuti munthu ulandire thandizo lachipatala cha boma mmaiko monga Zambia, Zimbabwe, Mozambique ndi Tanzania, umayenera kuonetsa chitupa chosonyeza kuti ndiwe nzika koma kuno kwathu izi sizichitika chifukwa kulibe ziphasozi. Monga akufotokozera Norman Fulatira yemwe ndi mneneri wa NRB, iyi mwina nkukhala mbiri yakale chifukwa Mmalawi weniweni azidziwika ndi chiphaso chomwe adulitse. Mavuto amenewa akhala mbiri yakale posakhalitsapa pamene ntchito yodula ziphaso za unzika yayamba. Gawo loyamba tayamba kupanga ziphaso za aphungu a Nyumba ya Malamulo, akuluakulu mboma, komanso midzi 27 mmaboma 11, adatero Fulatila. Mabomawa ndi Chitipa, Mzimba, Nkhotakota, Lilongwe, Salima, Dowa, Mchinji, Blantyre, Mangochi, Chikwawa ndi Thyolo. Zitupazo azidula mmidzi iwiri pa boma lililonse. Ili ndi gawo loyamba, gawoli likufuna lingotithandiza momwe ntchito ikhalire, ili ngati ntchito yoyeserera kaye koma anthu alandira ziphaso zawo. Mudzi ulionse takonza zoyamba ndi anthu 200 ndipo gawoli likamatha, anthu 5 000 akhala ndi ziphaso zawo, adatero mneneriyu. Iye adati gawo lachiwiri la ntchitoyi, anthu 95 000 ndiwo adzakhale ndi mwayi wokhala ndi ziphasozi ndipo gawoli likuyembekezereka kudzatha mu December chaka chino. Chaka chamawa, bungweli likuyembekezera kuti ntchitoyi idzafalikira dziko lonse pomwe anthu 9 miliyoni akuyembekezeka kulandira zitupa zawo. Fulatira adati aliyense amene wakwanitsa zaka 15 ndiye akuyenera kudulitsa ziphasozi. Iye watinso ngati uli nzika ya dziko lino, uyenera kudulitsa ziphasozi posatengera zikhulupiriro zako kapena mpingo. Naye mkulu wa bungwe loona zaumoyo la Malawi Health Equity Network (Mhen) George Jobe wati ntchitoyi ipindulira Amalawi komanso boma. Apapa ndiye kuti thandizo la mabungwe ndi boma lizipitadi mmanja mwa Amalawi enieni kusiyana ndi poyamba pamene timaphangirana ndi obwera, adatero. Kwa amene ataye chiphasochi akuti ayenera kudzalipira K3 500 kuti amupangirenso chiphaso china. Koma malinga ndi Fulatira, mtengowu ukhala ukusinthasintha. ",2 "Ophunzira Akatolika pa CHANCO Akhazikitsa Mlozo Wolemba: Thokozani Chapola tent/uploads/2019/11/bishop-tambala.jpg"" alt="""" width=""306"" height=""357"" />Wayamikira ophunzira a katolika pa Chancellor College-Bishop Tambala Episikopi wa mpingo wa katolika mu diocese ya Zomba Ambuye George Desmond Tambala wayamikira ophunzira a mpingo wa katolika kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor kamba kokhadzikitsa mulozo (Stratrategic Plan) woti uwathandize kupititsa patsogolo ntchito zotukula mpingowu ndi chikhristu chawo ku sukuluyi. Ambuye Tambala amayankhula izi pa mwambo wokhazikitsa mulozowu ku sukulu-yi. Iwo alimbikitsa mgwilizano wabwino pakati pa ophunzira-wa ponena kuti kuchita izi ndi komwe kungathandizire ophunzira-wa kuti athe kukwanilitsa mapulani a ntchito zawo potsatira mulozo-wu. Poyankhulapo yemwe adali mlendo wolemekezeka pa mwambo-wu Dr. Mary Shawa analimbikitsa ophunzira-wa pa za moyo wawo wa uzimu. Mmau ake mmodzi atsogoleri a aophunzira achikatolikawa Gift Muyayi wati ngati ophunzira ayesetsa kukwanilitsa mapulani a ntchito zosiyanasiyana omwe ali mu Strategic Plan imeneyi. Pa sukulu ya Chancellor College pali ophunzira pafupi fupi 2000 omwe ndi ampingo wa katolika. ",3 " Kuchitsedwa ntchito ndi zina Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mourinhao ndi mmodzi mwa anzanga amene ndimacheza nawo pa Wenela. Sindikudziwa kuti nchifukwa chiyani mkuluyu amakonda Arsenal. Momwe amaonekera, nzeru zake, ndimadabwa kuti iyeyu ndi Arsene Wenger adadyetsana mankhwala a mtundu wanji. Nchifukwa chake nthawi zambiri tikamukumbutsa kuti patha zaka 10 timu yakeyo isanachite zakupsa potenga chikho amakwiya zedi! Koma iyo ndi nkhani ya tsiku lina. Tsono Mourinhao adatopa ndi kuitanira minibasi, ndipo adapempha mwini minibasi ina kuti amupezere ntchito. Mwini minibasiyo adali dotolo. Pambali pothandiza odwala ku Gulupu, dotoloyo amakaphunzitsanso kusukulu ina ya anamwino. Apa zili bwino Tade. Kukhosi kwanga kuchita kusalala. Bakhalani ndi kuitanira kwanuko mpaka day yobwera Yesu. Uku kukumakhala kudya za tswayitswayi osati masewera, adandiuza tsiku lina atatizungulira pa Wenela. Koma ngati adathako sabata zitatu? Ndidangoona akubwera tsiku lina atazyolika. Bwanjinso nanga? ndidamufunsa. Ndailephera ntchito. Andichotsa, adayankha mwa chidula. Apa mpomwe adafotokoza momwe ntchitoyo idathera. Ndimagwiranso ntchito yokonza mnyumba mwa dotoloyo: kukolopa, kusesa, kukonza mufiliji ndi zina zotero. Tsiku lina, ndidapeza kuti liver ina idakhalitsa mfilijimo. Ndidaaitenga kukaotcha kunyumba. Atabwera mkulu uja adandifunsa: Ndinasiya katundu umu, watenga ndani? Ndipo ndidati sindikudziwa, adafotokoza mkulu uja. Adamezera malovu, nkupitiriza: Nthawi ya nkhomaliro adandifun-sanso, ndidakananso. Ngakhalenso madzulo adandifunsa ngati ndidaona katundu wake, ndidakananso. Pobwera madzulo tsiku linalo, adabwera ndi mowa umene adandigaila. Akuti mkuluyo ataona kuti Mourinhao wayamba kuledzera adamufunsanso: Ndinasiya katundu wanga. Watenga ndani? Ndipo Mourinhao adayankha: Mukunena nyama ija? Ndaotchera, pepani. Mkulu uja adangoti: Chinalitu chiwindi cha munthu ndimati ndikaphu-nzitsire. Abale anzanga, tikakhala pantchito sib wino kusolola ngakhale zimene tikuziona kuti nzazingono. Tikadakhala kuti tonse tilibe mtima osolola, nkhani ngati zotengera abale ndi alongo kunja moononga ndalama, kubwereka ndege yaufiti ngati kabanza si bwenzi zikutisautsa. Hallo Tade, wasowatu. Ndalanga wina uku, adatero Abiti Patuma, msungwana wosowa ngati Adona Hilida pano pa Wenela. Zinakhalanso bwanji? adafunsa Gervazzio, mmalo moika nyimbo ya Nakulenga. Amakula mtima, ati mkazi wake amamukhulupirira koopsa ndipo iyeyo kanali koyamba kuti apusitse mkazi wakeyo pocheza ndi ine. Poti anali ataledzera modziiwala, ndinatenga mapepala onse amagwiritsa ntchito nkuwaika mthumba la buluku, adatero Abiti Patuma. Adaonjeza kuti mawa lake, adangomva kuti ukwati wamkuluyo watha. ",7 "Boma Lapereka 35 Milion ku Khonsolo ya Dedza Khonsolo ya boma la Dedza yalandira ndalama zokwana 35 Million Kwacha kuchokera ku boma la Malawi zothandizira kuchepetsa kufala kwa matenda a COVID-19. Bulukutu: Atolankhani atithandize pofalitsa uthenga Bwanamkubwa wa bomali a Emanuel Bulukutu alankhula izi pamene khonsoloyi imaunikira atolankhani za mmene angalembere nkhani zokhudza matendawa. A Bulukutu ati ngakhale kuti khonsoloyi yayika ndondomeko zoyenera zodziwitsira anthu kapewedwe kamatenda-wa anawona kuti nkofunikira kuti atolankhani akhale patsogolo chifukwa wailesi zimafikira anthu ambiri mdziko muno. Tikufuna atolankhani akhale patsogolo potithandiza kufalitsa uthenga umenewu chifukwa wailesi zimafikira anthu ambiri mdziko muno, anatero a Bulukutu. Iwo ati mabungwe enanso monga World Vison, GIZ, United Purpose ndi ena athandizanso bomali ndi ndalama komanso katundu wosiyanasiyana. ",2 "Katswiri Wayamikira Nduna Zatsopano, Nduna Imodzi Yakana Udindo Katswiri pa nkhani za ndale mdziko muno Dr. Boniface Dulani wati ali ndi chikhulupiliro kuti nduna zomwe zasankhidwa ndi President wa dziko lino Dr. Lazarus Chakwera, zigwira ntchito zawo bwino popeza kuti zili ndi zowayenereza kugwira ntchitoyi. Dulani: Ndikukhulupilira kuti agwira bwino Dr. Dulani yemwenso ndi mphunzitsi wa zandale ku sukulu ya ukachenjede ya Chancellor, wauza Radio Maria kuti anthu ayike chikhulupiliro mwa ndunadzi pofuna kuti zigwire ntchito yawo bwino. Iwo ati mwachitsanzo, wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr. Saulosi Chilima, mu ulamuliro wa Professor Peter Mutharika mchaka cha 2014, adagwiraponso unduna ngati omwewu ndipo adagwira ntchito yawo mwaukadaulo. Tidikirebe kuti tiwone kuti akagwira ntchito yotani komano a Vice President tikuziwa tonse kuti anagwirapo ntchito mu undunawu ndipo anayigwira bwino ntchito, komanso mukuwuona kwanga boma lasankha ndunazi kuti chitetezo cha mkati mwadziko bwino chikhale choyenerera, anatero a Dulani. Msiska: Ziwoneka ngati akundipatsa mphatso Padakalipano yemwe anasankhidwa kukhala nduna yowona za chilungamo ndi malamulo a Modecai Msiska awukana udindowu ponena ena aganiza ngati a Chakwera akuwalipira pa ntchito yomwe anathandizira chipani cha MCP kuti chipambane pa mlandu wa chisankho cha president. Iwo anapitirizanso kunena kuti pali achinayamata ambiri omwe angati kugwira ntchito pa udindowu osati iwo omwe ndi achikulire. ",11 " Mugwiliranji bere la mwini? Masiku apitawa mtsikana wina adandifotokozera za momwe mphongo ina idagwirira bere lake pa msewu mumzinda wa Lilongwe. Mtsikanayu adali akungodziyendera mutauniyo pomwe adangodzidzimuka mkono wa bambo yemwe amabwera kutsogolo kwake uli pabere lake. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mmene amati azilankhula, bamboyo nkuti atayamba kuyenda kupitiriza ulendo wake ngati sadachite kalikonse. Mtsikanayo adangoti kakasi, kenaka adangopitiriza ulendo wake ali cheucheu kuti bambo wina asamuonererenso. Nkhaniyi idandikumbutsa zomwe zidandionekera mutauni ya Limbe, ku Blantyre, zaka zinayi kapena zisanu zapitazo. Anthu adali pilingupilingu mmawa wa Loweruka limenelo ndipo ndidali pandawala kukwakwera basi pomwe ndidangozindikira mkono wa mnyamata wina, yemwe ndidali ndisadamuoneko chibadwire, uli pabere langa. Ndikudzidzimuka, mnyamatayo, yemwe timayenda mosemphana, adapitirira ulendo wake akumwetulira ngati sadachite chilichonse chodabwitsa. Ndidangoti kakasi, kusowa cholankhula mnyamatayo akulowelera mgulu la anthu omwe anali akuyenda pamalopo. Amayi ndi atsikana omwe zangati izi zidawaonekerapo angachitire umboni za mkwiyo ndi manyazi omwe amadza zoterezi zikakuchitikira, poti ena zawachitikira mmaofesi, kusukulu ndi malo ena. Kwa nthawi yaitali ndidakhala ndikudzifunsa za mmene ndikadakhaulitsira ndoda yachipongweyo. Ndikadakuwa? Koma ndi changu chimene mnyamatayu adachita, ndimakaika ngati ena omwe amadutsa pamalopo adaona zomwe zidachitika. Akadandikhulipilira ndani? Umboni sukadavuta kodi? Kapena ndikadamumenya? Koma mwachidziwikire akadabwenzera ndipo mwinanso nkadavulazidwa ndine ndemwe. Ena nkumati atsikana mukumadziitanira mavuto nokha kaamba kamavalidwe kosadzilemekeza, koma ichi sichifukwa chokwanira mpangono pomwe choti anthu ena azichita zomwe afuna ndi matupi a amayi. Kaya wina atavala zoonetsa mawere ake, palibe choyenereza bambo kapena mnyamata kugwira mawerewo. Tisaiwale kuti mdziko muno muli ufulu wa kavalidwe. Kwa amayi, ndikukhulupilira kuti kungopenya ngati momwe ndidachitira ine ndi msungwana wa ku Lilongweyu, sikungathandize kwenikweni. Ngati pali chomwe mungathe kuchita kuti abambo oterewa aonekere poyera, chitani, kuti aone polekera. ",15 "Papa Wayamikira Akayidi a Ndende ya padua Mdziko la Italy Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wathokoza akayidi a pa ndende ya Padua mdziko la Italy. Papa pa umodzi mwa maulendo ake oyendera akayidi Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican, iye anathokoza akayidiwa pokonza mapemphero a njira ya mtanda ya chaka chino zomwe wati zawonetsa ukulu wa Mulungu pakati pawo. Pamenepa Papa wati apitiriza kupemphelera akayidiwo kuti Mulungu adziwatetedza mu njira zosiyanasiyana pomwe ali ku ndendeko. ",14 "Dziko la Turkey Likuthamangitsa Obwera jpg"" alt="""" width=""413"" height=""275"" />Anthu obwera akuwafanizira ndi zigawenga izi Dziko la Turkey layamba kuthamangitsa mzika za mmaiko ena zomwe likuziganizira kuti zikukhudzidwa ndi gulu la zauchifwamba la Islamic State. Malipoti a wailesi ya BBC ati ngakhale maiko ena aku Ulaya sakufuna kulanda ziphaso za umzika kwa anthuwa, koma maiko monga Germany, Denmark komanso United Kingdom alanda kale ziphaso kwa anthuwa omwe analowa gulu la zauchifwamba la Jihadists. Padakali pano dziko la Turkey likusungira asilikali mazanamazana ochokera mmaiko ena mu ndende zake ndi cholinga chakuti afufuzidwe bwinobwino ngati sakukhudzidwa ndi gulu la zigawengali. Kumayambiliro a mwezi uno boma la dziko la Turkey linatsindika kuti libweza asilikaliwa mmaiko a kwao ngakhale kuti anandidwa ziphaso za unzika wao. ",14 " Osaiwala kuteteza mtedza ku chuku Pamene mbewu ya mtedza yacha, katswiri wa mbewu za mtunduwu kwa Bvumbwe Richard Andasiki akuti alimi ateteze mbewuyi ku chuku pamene akukolola, kuyanika, kusenda komanso kusunga. Malinga ndi katswiriyu, mtedza umachita chuku mlimi akafulumira kapena kuchedwa kukolola, ukanyowa poyanika, mlimi akauviika mmadzi ndi cholinga choti asende mosavuta kapena akasunga pachinyontho. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mtedza wopanda chuku umayenda malonda Tisaiwale kuti tikapitiriza kukhala ndi mtedza wa chuku sitingakhale ndi mwayi wogulitsa ku maiko akunja choncho miyoyo yathu komanso dziko lathu silingatukuke. Chinthu china chomwe chikuyenera kutipatsa mantha nchoti chuku chimatulutsa poizoni yemwe amayambitsa matenda a khansa ndi kunyentchera, iye adatero. Kuonjezera apo, mphunzitsi wa ku nthambi ya za ulangizi wa mbewu ku Lilongwe University of Agriculture and Natural Resources (Luanar), Paul Fatch adati poizoniyu amachepetsa chitetezo cha mthupi komanso chilakolako cha zakudya. Poizoniyu akachuluka mthupi, amachepetsa mphamvu yobereka, adatero Fatch. Pofuna kupewa zonsezi, Andasiki adati choyambirira alimi akolole mtedza wokhwima bwino, akaukumba awuyanganitse kumwamba kufikira utauma ndipo akachoka apo, athothole ndikuuika mmatumba ndikusunga pouma. Katswiriyu adafotokoza kuti mlimi akolole mtedza akaona kuti mkati mwake makoko achita madontho akuda. Pofuna kutsimikiza izi, iye adati mlimi akuyenera kukumba mapando okwana 10 mwapatalipatali ndipo akamaliza, athothole mtedza ochepa pa phando lililonse ndikuwusenda. Mlimi akapeza kuti mwa mtedza 100 omwe waswa, wosachepera 80 makoko ake ali ndi madonthowa ndiyekuti wakhwima ndipo ayambe kukumba, adafotokoza motero. Iye adati pamene mlimi akukumba mtedza akuyenera kuwuzonditsa kuti uyangane kumwamba ndi cholinga choti uwume bwino ndi dzuwa. Mlangizi wa za ulimi wa mbewu ku Dowa Sangayemwe Kausiwa adati alimi akuyenera kusamala pokumba kuti wambiri usasalire mmunda. Poyambirira, iye adati mlimi apewe kudzula mtedza koma azigwiritsa ntchito khasu. Pokumba, mlimi aziima pakati pa mzere ndikukuma mbali zonse ziwiri mwa mphamvu ndi cholinga choti onse unyamuke bwino, adatero Kausiwa. Mlangiziyu adati kuyenda mmunda ndikumatolera osalira kumathandizira kuti pafupifupi mtedza wonse uchokemo. Iye adaonjeza kuti alimi apewe kuviika mtedza mmadzi kuti usavute kuswa chifukwa izi zimakolezera chuku. Andasiki adafotokoza kuti alimi apewe kusunga mtedza wosenda kwa nthawi yaitali chifukwa umaonongeka. Malo wosungira mbewuyi akhale ouma komanso alimi ayiteteze ku makoswe, adatero katswiriyu. Moses Tanazio wa mboma la Ntcheu ndi mmodzi mwa alimi omwe amatsatira bwino kwambiri malangizo pa ulimi wa mbewuyi. Iye adati padakali pano sadayambe kukolola kufikira ukwaniritse zomwe alangizi adamuuza. Mtedza wanga ukakhwima, ndimakumba ndikuuyanika mmunda momwemo powuzondotsa ndipo ndimathothola pokhapokha ukauma bwino. Mtedza owuma bwino umachita phokoso ukamautafuna choncho ukafika apa, ndimathothola, kuusankha, kuulongeza mmatumba abwino ndikuunga, iye adatero. ",4 "Zomba District Health Office launches its strategic plan. By : Judith Sonkho Formulation and implementation of a Strategic Plan (SP) is said to be one of the key ways and interventions for addressing a number of Health issues gripping the country. Acting Director of Health and Social Services in Zomba district, Dr. Raphael Piringu was speaking at a media briefing organized by Zomba District Health Office with an aim of updating journalists on the progress of their Strategic Plan implementation in the district. Dr. Piringu, said for the first time in the history of the Ministry of Health in the country, Zomba District Health Office launched its first-ever Strategic Plan to address a number of challenges affecting delivery of quality Health Care Services in the district. We are intensifying the fight against maternal mortality rate, infant mortality rate and fertility rate, among other thematic areas of this Strategic Plan, said Dr. Piringu. Acting Director of Health and Social Services in Zomba district, Dr. Raphael Piringu The Acting Director of Health and Social Services said maternal mortality rate is on the increase in the district, thereby fueling maternal deaths, and their target is to reduce the vice by 20 percent by the year 2022. According to Dr. Piringu, the SP will also be looking into a global problem of HIV/AIDS and Tuberculosis, but at district level. He also said his office will strengthen partner collaboration and community ownership of the Strategic Plan to ensure effective implementation of the same to achieve desired goals. As one way of strengthening this, we have formed the SP together with the community and the stakeholders and we are planning to implement and review it together, continued Dr. Piringu. The Strategic Plan has a lifespan of five years, from 2017 to 2022 and will be drawing its inspiration from the Ministry of Healths Strategic Plan which is currently being implemented at a national level. ",6 "Alimbikitsa Achinyamata Asamalire Chilengedwe Achinyamata a mu parish ya Bembeke mu dayosizi ya Dedza awapempha kuti athandize mpingo poteteza chilengedwe. Mkulu wa achinyamata mparishiyi a Ignasicius Chalanda ndi omwe amalankhula izi potsekera mbindikiro wa masiku atatu omwe anali nawo, pofuna kuwawunikira achinyamatawa zakuipa kowononga zachilengedwe. A Chalanda awunikiranso achinyamata kuti azigwiritsa ntchito makina a computer moyenera pofuna kupewa zinthu zoipa zomwe zikufalitsidwa kudzera pa makinawa. Tikuwasula kuti akhale achinyamata odalilika mu mpingo. Tikuwalimbikitsanso kuti atenge mbali posamalira chilengedwe, anatero a Chalanda. Polankhulapo mmodzi mwa achinyamata omwe anatenga nawo gawo pa mbindikirowu Olifeyo Christiano anati wapindula kwambiri ndi mbindikirowu. Tazindikira ntchito zomwe tikuyenera kuchita ngati mbali yathu mu mpingo, anatero Christiano. Iye wati pa mbindikirowu achinyamatawa alimbikitsidwanso kuwerenga kwambiri baibulo monga chaka chomwe Papa anakhazikitsa kuti chikhale cha baibulo. ",18 "Kawangi CDSS Iyendera ndi Kuthandiza Radio Maria Malawi By Richard Makombe Akhristu mdziko muno awalimbikitsa kuti azitenga nawo mbali pothandiza Radio Maria Malawi kamba koti imasowa thandizo pa ntchito yake yofalitsa uthenga wa Mulungu. Patron wa achinyamata a gulu la Young Catholic Students (YCS) pa sukulu ya Kawangi CDSS mboma la Dowa a Emmanuel Maseko ayankhula izi pomwe anadzayendera ku Radio Maria Malawi. A Maseko ati ndiokhutira ndi momwe Radio Maria imagwilira ntchito zake choncho nkoyenera kuti akhristu aziyithandiza kuti ipitilize kugwira ntchito zake. Ndife okhutira ndi kagwiridwe ntchito ka wayilesiyi ndipo tikuona kuti wayilesiyi imadzipereka pogwira ntchito zake choncho ndikoyenera kuyithandiza kuti ipitirize ntchito yabwino yomwe ikugwira, anatero a Maseko. Mmawu ake mmodzi mwa achinyamatawa Ezara Lazaro wati waphunzira zambiri paulendo wake ku Radio Maria, ndipo wati wadziwa zambiri za momwe wayilesiyi imagwilira ntchito zake. Ndikufuna ndipemphe achinyamata anzanga kuti nawonso tsiku lina adzabwere kuno kudzaona momwe wayilesiyi imagwilira ntchito zake komanso kudzaithandiza chifukwa ikusowekra thandizo la wina aliyense, anatero Lazaro. Achinyamatawa apereka ndalama zokwana 10 thousand kwacha kuti zithandize kupititsa patsogolo ntchito za wayilesiyi. ",13 " Makanja aphofomoka Makanja, chilombo chomwe chimayenda monyangwa poti chimayangana wina aliyense pamutu kaamba kotalika, chidaona zakuda masiku apitawa chitagwa pamsonkhano wa nduna ya zamalonda. Pomwe pabwera guleyu anthu amayembekeza kusangalala chifukwa amaoneka modabwitsa komaso amavina modolola mtima. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Izi zidali chomwecho Lachiwiri ku Wovwe mmboma la Karonga, komwe nduna ya zamalonda Joseph Mwanamvekha, kazembe wa dziko la Japan ku Malawi, Shuichiro Nishioka ndi alendo ena olemekezeka adakayendera alimi a mpunga. Pofuna kuti alendowo asangalale, anthu kumeneko adakonza magule. Ataitanidwa, makanja anabwera pamalo a msonkhano monyangwa. Guleyu adayendera pabwalo modzithemba asanayambe kuvina. Apa anthu adayembekezera kuti patuluka fumbi koma zachisoni guleyu atangoyamba kuvina adapeperuka ndi kugwa chagada mwendo umodzi utathyoka. Pofuna kudzichosa manyazi guleyo, adayamba kunamizira kuvina pansi koma anthu otsogolera guleyo adaona kuti zavuta ndipo adapita kukamudzutsa. Kaamba ka ululu ndi manyazi, guleyo adachoka mbwalo motsimphina ndi kukatsamira galimoto ya nduna kwinaku akumverera ululu. Guleyu adaoneka wosowa mtendere kaamba koti anzake anatenga malo nkuthyola dansi mododometsa kwinaku akufupidwa ndi nduna ndi kazembe wa ku Japan. Anthu odzigwira adamumvera chisoni makanjayo, koma aphwete adaseka kaamba koti zidali zachilendo kuona makanja akuthyoka mwendo gule ali mkati. Utatha msonkhano nkhani idali pakamwa idali ya kuphofomoka kwa makanja. Ngakhale Mwanamvekha ndi anthu a ku unduna wake, komaso DC wa boma la Karonga, Rosemary Moyo, sadapirire koma kukambirana za kugwa kwa gule wamtaliyo. Mwanamvekha adati chidali chinthu chodabwitsa komaso chanchilendo kwa iwowo kuona gule akugwa. ",19 "HRC Yati Ithandiza Pomenyera Ufulu wa Ofalitsa Nkhani Bungwe lowona za maufulu a anthu mdziko muno la Human Rights Commission lati liwonetsetsa kuti likuthandiza pomenyera maufulu a wanthu pa ndondomeko ya zofalitsa nkhani kuti asapitilire kuphwanyidwa. Semphere: MACRA izibwera poyera Mkulu wa bungweli a Patrick Semphere wanena izi pambuyo pa mkumano womwe bungweli lachita ndi bungwe la loyanganira nyumba zofalitsa nkhani mdziko muno la Malwi Communication Regulatory Authority (MACRA), komanso unduna wa zofalitsa nkhani. Iye wati bungwe la MACRA likuyenera kugwira ntchito mosakondera kuti ntchito yolemba ndikuwulutsa nkhani ipite patsogolo. Pamene pali madandaulo a nyumba yowulutsa mawu ina, MACRA izibwera poyera ndi kuthandiza pa madandaulo amene alipo monga mmene anthu amadandaulira anthu kwambiri nkhani ya mapologalamu a pa MBC, anatero a Semphere. Pa zokambiranazi bungwe la bungwe la Human Rights Commission (HRC) lapempha bungwe la MACRA kuti lidzigawana malipoti a ntchito zawo ndi bunweli, komanso lilimbilitse mabungwe ena kuti adzigwira nayo ntchito limodzi pofuna kuti ntchito zake zizikhala zokomera wina aliyense. ",14 " Mkangano pakati pa asilamu ndi a gule Mkokemkoke udakula ku Mitundu mumzinda wa Lilongwe Lamulungu lathali pomwe a gule wamkulu adayamba kukokanakokana ndi anthu a chipembedzo cha Chisilamu. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mkokemkokewo udayamba pomwe kudamveka kuti kuchipatala china kumeneko mayi wina wabereka mwana wokhala ngati gule wamkulu. Izo zidachitika mwamuna wina yemwe ati ndi mwamuna wa mayiyo adakatentha zibiya za gule wamkulu. Apa a kudambwewo adalamula Asilamuwa kuti apereke ngombe zisanu, akapereke phulusa la zomwe adatenthazo kwa mfumu komanso kuti avinire achinyamata Achisilamu omwe adakhudzidwa ndi nkhaniyo. Nkhaniyi pano ili mmanja mwa bwanamkubwa wa Lilongwe, Paul Kalilombe, yemwe wati adakumana ndi mbali ziwirizi ndipo pali chiyembekezo kuti iwo asiye kumenyana. Kalilombe wati mbalizi zauzidwanso zolemekeza chikhalidwe komanso chipembedzo cha aliyense malinga ndi malamulo adziko lino. Naye mlembi wa mkulu wa gulu la Achewa la Chewa Heritage Foundation (Chefo), Amos Chinkhadze, adatulutsa chikalata chopempha mbalizi kuti zisiye kuponyerana Chichewa ndikulola zokambirana kuti zichitike. ",13 " Chisiki: Mchezo wa amayi Chikondano: Amapatsana zinthu mwachinsinsi Pamoyo wathu pali njira zambiri zomwe timalumikizirana pophunzitsana, kugawana nzeru ndi kuunikirana. Umu ndimo moyo ulili. Ngakhale izi zili choncho, ambiri amaona ngati okhala nawo pafupi ndiwo angakhale abwenzi awo, koma maganizo oterewa akutsutsidwa ndi mchezo wa amayi womwe amautcha chisiki. Ndidacheza ndi Miriam Chikondano, yemwe akulongosola za chisiki motere: Moni mayi ndipo ndikudziweni. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Zikomo, bambo. Ine ndili bwino ndipo dzina langa ndine Miriam Chikondano wammudzi mwa Chimoka ku Lilongwe. Ndili pabanja ndipo ndili ndi ana 4anyamata atatu ndi msungwana mmodzi, mzime. Mudapalanako ubwenzi ndi mayi mnzanu? Kwabasi, moti padakalipano ndili ndi abwenzi achizimayi ambiri zedi omwe ndimagawana nawo nzeru ndi kucheza nawo. Ubwenzi woterewu mumawuona bwanji? Choyamba ndimasulire tanthauzo la mawu akuti ubwenzi chifukwa masiku ano anthu amaganiza mothamanga ndiye ena amadzayamba kutanthauzira mawuwa mwawomwawo. Mawu akuti ubwenzi amatanthauza chinzake pakati pa anthu awiri kapena kuposerapo. Mukafunsa za mmene ndimauonera ubwenzi woterewu yankho langa ndi lakuti ndi njira imodzi yabwino kwambiri yomwe anthu amagawanirana nzeru, kulangizana ndi kulumikizana pankhani zosiyanasiyana. Kodi mgwirizano wa amayi umatchedwa kuti chiyani? Mgwirizano wa amayi umatchedwa kuti chisikileti koma mwachidule amangoti chisiki ndipo mzimayi mmodzi amatha kukhala ndi zisiki zingapo panthawi imodzi popanda vuto kapena madandaulo alionse. Dzinali limachokera pati? Dzinali lisakuzunguzeni, ayi, limachokera pa mawu Achingerezi oti secret koma ndi longofuna kusiyanitsa maubwenzi ena ndi ubwenzi umene tikukambirana panowu. Dzinali limabwera potengera zomwe zimachitika paubwenziwo. Apa ndikutanthauza zomwe mayi ndi bwenzi kapena abwenzi ake amapangirana paubwenzi wawo. Mungatambasule zomwe zimachitikazo? Panthawi ya ubwenziwo amayi amagulirana mphatso zosiyanasiyana mwamseri nkumapatsana mokhala ngati mobisa zija mChingerezi amati secret monga ndanena kale, ndiye pofuna kusazungulira amangoti chisiki basi. Chisiki chimayamba bwanji? Pali njira zambiri zomwe chisiki chimayambira koma mfundo yaikulu yagona pakuti anthuwa amakhala paubwenzi. Chisiki china chimayamba chifukwa anthu amachokera kumodzi, china chimayamba chifukwa chakuti anthu amayendera limodzi kapena adakumana kumalo kapena kuzochitika zina zake monga kutchalitchi, kumpalano wa magule, kumsonkhano ndi malo ena. Ndiye zimayamba bwanji? Ngati anthu agwirizana magazi amatha kukambirana kuti ayambe chisiki koma nthawi zina wina amangoyamba kutumizira mnzake mphatso kenako winayo amabweza basi chisiki chayamba chikatero. Phindu lake ndi lotani? Pali phindu lalikulu kwambiri, makamaka pamoyo wa munthu wamayi. Amayi amakhala ndi nkhawa komanso milandu yambiri mumtima kuposa abambo ndiye ngati mzimayi alibe mnzake womukhuthulira nkhawa ndi milandu yotere, moyo wake umakhala wokwinyirira ndiponso zinthu siziyenda koma akakhala ndi mnzake ngati siki wake amatha kukhuthulira khawa ndi mavuto otere kwa mnzakeyo, mtima nkumapepuka. Basi phindu lake nkukhuthula nkhawa ndi mavuto? Ayi, chomwe ndikutanthauza nchakuti pamakhala nkhawa ndi madandaulo ena ofunika kutanthauziridwa kapena kulimbitsidwa mtima ndiye amayi awiriwo pausiki wawo amakhala pansi nkukambirana za nkhani ngati zimenezi nkuthandizana nzeru kuti zinthu ziziyenda mndondomeko yake. Nanga chisiki chimatha kapena nchamuyaya? Chikhoza kutha malingana ndi zifukwa zake koma osangoti kwacha mmawa basi nkumati ndikuthetsa chisiki popanda chifukwa kapena mlandu uliwonse. Chifukwa chachikulu chagona pakusungirana chinsinsi monga ndanena kale kuti amayi omwe ali pachisiki amatha kuuzana za mavuto osiyanasiyana okhudza moyo wawo ngakhalenso a mbanja. Ndiye ngati wina akunka nalengeza za mavuto a mnzake chisiki sichingapitirire chifukwa palibenso ulemu kapena chinsinsi. Mungawauze chiyani amayi za chisiki? Mawu ndiwochepa. Mpofunika kusamala posankha bwenzi la chisiki basi. Ndi bwino ukaona kuti mnzako ali ndi chidwi choti mukhale pachisiki kumufufuza bwino lomwe kupewa kuti mudzayambane nkudana patsogolo. ",15 "Madise Walangiza Makomishonala Atule Pansi Maudindo Awo Mmodzi mwa akatswiri pa nkhani za malamulo mdziko muno Dr. Sunduzwayo Madise walangiza makomishonala a bungwe loyendetsa chisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) kuti atule pansi maudindo awo. Dr. Madise yemwenso ndi mphunzitsi wa za malamulo ku sukulu ya ukachenjede ya Chancellor amayankhula izi pothilirapo ndemanga pa zomwe wanena mmodzi wa ma Commissioner a bungwe la MEC, Dr. Jean Mathanga pa msonkhano wa atolankhani lachiwiri, pomwe anati sangatule pansi udindo wake pokhapokha contract yake itatha. Odziwa ntchito mdziko muno si okha-Madise Iwo awuza ma Commissioner kuti ntchito yomwe akugwira siyawo koma ndi yothandidza mtundu wa a Malawi choncho sipofunika kuti akakamilire kugwira ntchito. Akuyenera kudziwa kuti ntchitoyi ndi yotumikira a Malawi ndipo ngati zavuta, yawavuta ndi ofesi ya ukamishonalayo osati alephera ndi iwowo ngati munythu ayi, anatero Dr. Madise. Pamenepa Dr. Madise atinso ngati makomishonalawa akakamirebe kudzayendetsa chisankho chikubwerachi ndiye kuti padzakhalanso mpungwepungwe chifukwa anthu sadzawakhulupiliranso. Apapa kukakamiraku akungopereka mpata wa mpungwepungwe winanso. Mdziko muno odziwa ntchito si okha ayi akanasiya maudindo ena ayendetsenso, anatero Dr. Madise. ",11 " Alowerera paesiteti ya Kawalazi T/A Kabunduli wa mboma la Nkhata Bay wadandaula ndi anthu pafupifupi 500 omwe adalowerera ndi kukhazikika paesiteti ya tiyi ya Kawalazi mbomalo. Kabunduli wati anthuwa, omwe awutcha mudziwo Joni(potengera mzinda wa Johannesburg mdziko la South Africa), ndi aupandu chifukwa sadatsate dongosolo loyenera lopezera malo. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Anthuwa adandipeza zaka zoposa zisanu zapitazo kupempha malo ndipo ndidawauza dongosolo loyenera, koma zodabwitsa ndi zoti adakalowerera malo a esiteti, adatero Kabunduli. Mwambi uja amati tikhale nawo adalanda malo ukupherezera pankhaniyi pomwe Kabunduli akulongosola kuti anthuwa si mbadwa za boma la Nkhata Bay koma ndi obwera kuchokera maboma ena a mhigawo cha kumpotochi. Kabunduli adati ali ndi nkhawa ndi mkanganowu chifukwa esitetiyi ndi mpamba wa anthu ake. Ndikuopa kuti mkanganowu ungakhudzenso ntchito za anthu a mdera langa amene amagwira kuesitetiku, Kabunduli adatero. Ndipo DC wa bomali, Fred Movete, adati anthuwa, omwe ambiri mwa iwo amaotcha makala chifukwa derali lili ndi mitengo yachilengedwe, amati adalowerera malowa chifukwa omwe adagula esitetiyi mzaka za mma 1970 sanawapatse makolo awo chipepeso. Movete adati ngakhale anthu ena akutero, ofesi yake idalandiranso malipoti oti anthuwa si mbadwa za mboma la Nkhata Bay koma ochokera kumaboma ena. Iye adalongosola kuti nkhaniyi yakhala ikulowa mbwalo la milandu kangapo konse makamaka pomwe anthu olowererawa adaphwanya galimoto, kulanda wapolisi mufti (yomwe idapezeka) ndi kuvulaza ogwira ntchito pakampaniyi. Padakalipano, tikukambirana ndi mbali ziwirizi kuti tibweretse mgwirizano chifukwa nkhanizi zikafika kukhoti, zinthu zimaonongeka, adatero Movete. Poyankhulapo akuluakulu a esitetiyi adati mchitidwewu ndi wobwezeretsa chitukuko mmbuyo. Wachiwiri kwa mkulu wa kampaniyi, Kenneth Kabaghe, adati anthuwa aika kampaniyi pampani. Iye adati ncholinga cha kampani yake kukhala mwabata ndi anthu oizungulira, koma izi zikuvuta ndi anthu a mudzi wa Joni. ",7 " Kukana kuba Woimba Joseph Nkasa mnyimbo yake ina, amaneneratu kuti aliyense ayenera kugwira ntchito ina iliyonse kupatulapo kuba. Ngakhale Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi sunganeneretu kuti kuba ndi ntchito, kupewa tchimoli kuli ndi njira zambiri. Apa tikuona mnyamata wina kumsika wa Limbe kugulitsa zinkhupule poopa kuba. Ntchito nzosiyana, koma tisaiwale ndalama ndi imodzi. ",9 " Mai Mutharika ati amayi akhale odzidalira Mkulu wa bungwe la Beautify Malawi Trust (Beam Trust), Gertrude Mutharika, walimbikitsa amayi mdziko muno kuti akhale odzidalira pachuma. Mutharika adalankhula izi masiku apitawa pomwe amakhazikitsa tsiku lokumbukira ntchito za mabizinesi la World Entrepreneurship Day mdziko la Amerika. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mutharika: Tayika ndondomeko zingapo Mutharika adati Beam Trust ikufuna kulimbikitsa amayi kutengapo gawo lalikulu pantchito za mabizinesi ngati njira imodzi yowalimbikitsira kudziyimira paokha. Tayika ndondomeko zingapo zomwe cholinga chake nkupititsira amayi ndi atsikana mmabizinesi. Beam Trust ilimbikitsanso amayi ndi atsikana kutengapo gawo lalikulu pantchito zolimbikitsa ukhondo mmatauni ndi mizinda, adatero iye. Iye adatsindika kuti kusowa mpamba woyambira bizinesi ndi chikole ndiye mavuto amene amayi ndi asungwana omwe akufuna kuyamba mabizinesi akukumana nawo mu Africa. Choncho, iwo adapempha mabungwe omwe ndi mabanki kuti aganizire kufewetsa mfundo zawo kuti amayi ndi atsikana adzitha kupeza ngongole mosavuta. Ena mwa atsogoleri omwe adakhala nawo pamsonkhanowo ndi mkazi wa pulezidenti wa ku Namibia Penehupifo Pohamba ndi mkulu wa bungwe la UN Foundation Cathy Calvin. ",11 "Papa Wapempha Anthu aku Japan Amupempherere Wolemba: Sylvester Kasitomu Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco wapempha anthu a mdziko la Japan kuti ateteze moyo komanso apemphelere ulendo wake wopita mdzikolo. Papa walankhula izi lero kudzera pa uthenga wake wa kanema ndipo wati chitetezo chomwe iye akupempha ndi chochokera mu mtima. Pamenepa Papa wati akukhulupilira kuti anthu a mdziko la Japan amazindikira ubwino wokambirana ngati pali kusamvana ndi cholinga chofuna kuteteza umoyo wa anthu. Iye anati dziko la Japan ndi lodalitsidwa ndi chikhalidwe chabwino chomwe chimasonyeza umoyo wabwino. Pomaliza mtsogoleri wa mpingo wakatolikayu anayamikira onse omwe akuchita dongosolo lokonzekera ulendo wake ndipo anati apitiliza kupemphelera aliyense. ",13 "Papa Wayamikira Asisiteli a Chipani cha Vincent De Paul Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wayamikira asisiteri a chipani cha Vincent De Paul Woyera kamba ka ntchito yotamandika yomwe akhala akugwira ku likulu la mpingowu ku Vatican. Asisteri a chipani cha Vincent de Paul Woyera Papa Fransisco walankhula izi loweruka pa Misa yomwe anatsogolera kulikulu la mpingo ku Vatican. Iye wayamika asisiteliwa chifukwa cha ntchito yawo yomwe amagwira potumikira modzipereka ndimosatopa ndipo wati Tiwapemherere kuti Mulungu awapatse chaulere kamba ka ntchito yomwe amagwira. Chakachi poyamba chimachitika pa 15 March koma chinasinthidwa ndipo chimachitika pa 9 May mu nyengo ya Pasaka. ",13 "Anthu Okwiya Apha Munthu Pomuganizira Kuti Waba Mbuzi Bambo wina wa zaka 28 zakubadwa wa mboma la Chikwawa, waphedwa ndi anthu ena okwiya pomuganizira kuti anaba mbuzi. Wachiwiri kwa wofalitsa nkhni za apolisi mboma la Chikwawa Sergeant Dickson Matemba wati 11 koloko ya usiku wa tsikuli, mkuluyu Paul Fulyton amayendetsa njinga yamoto atanyamula mbuzi yokupha kale ndipo anthu ena a mmudzi mwa Nsanjama atamufunsa anakanika kufotokoza bwino za komwe watenga mbuziyo. Izi zinachititsa kuti anthuwo ayambe kumumenya ndipo kenaka anamuyatsa iye pamodzi ndi njinga yamotoyo. Apolisi ndi a zachipatala anafika pamalopo ndipo zotsatira za ku chipatala ati zasonyeza kuti mkuluyu wafa kaamba kotaya magazi ambiri chifukwa cha kuvulazidwa mmutu. Padakalipano apolisi mbomalo achenjeza anthu kuti aleke kutengera malamulo mmanja mwawo ndipo mmalo mwake azikanena ku polisi nkhani iliyonse yomwe yachitika ku dera kwawo. ",14 " Kusanthula ulamuliro mmasiku 100 a Banda Boma la mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda, likuyenera kukhwimitsa chitetezo mdziko muno, kuchepetsa kumanga anthu chisawawa komanso kuchepetsa kuchotsa anthu pantchito. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Atsogoleri azipani, mabungwe, mafumu komanso anthu otumikiridwa atero msabatayi pomwe amaikira ndemanga pazomwe mtsogoleriyu wachita mmasiku 100 akulamulira dziko lino. Koma mneneri waboma, Moses Kunkuyu, wati kusintha kwa maundindo ndi ntchito zina sikolakwika chifukwa mtsogoleri wa dziko akamalowa pampando amasankha anthu oti agwire nawo ntchito. Nayo nduna yazamdziko, Uladi Mussa yati boma likuyesetsa kuti chitetezo chikhwime mdziko muno. Iye adati nkutheka alipo ena omwe akufuna kuti ayalutse boma la Banda kuti lilibe chitetezo. Posangalala kuti watha masiku 100 akulamula dziko lino kuchokera pa 7 Epulo pomwe adamulumbiritsa mtsogoleri wakale wa dziko lino Bingu wa Mutharika atamwalira mwadzidzidzi, kudali mapemphero komanso zochitika zosiyanasiyana. Banda adayamba kulamula dziko lino litakutidwa mmavuto ndi mikwingwirima monga kusowa mafuta, ndalama zakunja, shuga ndi zina zotere. Nthawi ya ulamuliro wa Mutharika ndi chipani chake cha Democratic Progressive Party (DPP) kudadzanso malamulo ena amene amaoneka kuti ndiopondereza, monga lamulo limene limapatsa mphamvu apolisi kuchita chipikisheni opanda chikalata chaboma, lamulo lopereka mphamvu kwa nduna kutseka nyuzipepala kapena wailesi yodzudzula boma komanso kusokonekera kwa ubale wa dziko lino ndi maiko ena. Banda ndi chipani chake cha Peoples Party (PP) atangotenga boma, mavuto enawo adazilala. Koma malinga ndi ena, bomali lili ndi zolakwika zake. Manthu a mavuto Mneneri wa DPP, Nicholas Dausi, wati pamasiku 100, chipani chawo chaona zokhoma, manthu wamavuto komanso kulira chifukwa cha mpanipani womwe Banda wauchita kwa anthu achipanichi. Dausi wati sakuona chifukwa chomwe Banda angaonongere chuma cha boma posangalala kuti watha masiku 100 chikhalirecho zinthu mdziko muno sizili bwino. Chisangalalocho chikudabwitsa, kodi akusangalalira kuti Bingu adamwalira? Sitikuona kuti pali chosangalalira chifukwa ngakhale akuti mdziko muno muli mafuta komanso ndalama zakunja, moyo wa munthu wakumudzi sudasinthe chifukwa zinthu ndiye zakwera mtengo, adatero Dausi. Iye adati mdziko muno anthu achotsedwa ntchito komanso kumangidwa. Adapereka zitsanzo za omangidwa: mkulu wa bungwe lothana ndi ziphuphu la Anti-Corruption Bureau (ACB) Alexious Nampota, gavanala wa DPP kumpoto Christopher Ngwira, mkulu wa achinyamata mu DPP Lewis Ngalande, kalaliki wamkulu wa Nyumba ya Malamulo Matilda Katopola, mkulu woyanganira nyumba zaboma Edward Sawerengera ndi wachiwiri wake Nector Mhura, mkulu wapolisi Peter Mukhito komanso mkulu wa banki ya Malawi Savings Bank. Boma lakana kulembanso ntchito yemwe anali mkulu wa nthambi yaboma yoona za olowa ndi kutuluka mdziko muno Elvis Thodi. Kuchotsana ndi kumanganaku kukutidabwitsa, adatero Dausi. Mneneri wa chipani cha UDF, Mahmudu Lali, wati kupezeka kwa mafuta agalimoto, ndalama zakunja, kuchotsedwa kwa malamulo oipa komanso kubwezeretsedwa kwa mbendera ya dziko lino kwasonyeza kuti utsogoleri wa Banda zinthu zayamba bwino. Koma Lali wati boma lisakomedwe chifukwa zina zayamba kale kusokonekera: Chitetezo chasokonekera, taonanso momwe bomali layendetsera gawo 65 la malamulo adziko lino kuti angochita momwe boma la DPP lidachitira. Litawonanso kuti zipangizo zophunzirira ndizokwana msukulu komanso masitalaka akuyenera kutha. Zikuyenda bwino Malinga ndi kusintha kwa boma, aphungu ena achipani cha DPP adakhamukira kumbali ya boma mnyumba ya malamulo, koma ngakhale malamulo amati aphungu otere achitsedwe pamipando yawo ndipo kukhale chisankho cha chibwereza, Banda komanso akuluakulu a DPP ati izi nzosayenera chifukwa zingaononge ndalama komanso chifukwa boma lokhazikika ndilo likufunika. Mkulu wa bungwe loona zaumoyo la Malawi Health Equity Network (MEHN) Martha Kwataine wati ngakhale masiku 100 ndiochepa kukonza zinthu, boma la Banda layesetsa. Iye wati Banda akuyenera kuchenjera ndi anthu omwe amuyandikira chifukwa ndi anthu omwewo omwe adayandikira Mutharika. Tipemphe kuti bungwe la ACB lizifufuzanso anthu omwe ali mboma osangoti lidzifufuza omwe siali mboma, adatero Kwataine. T/A Chekucheku ya mboma la Neno yati sabata yathayi kwawoko amalandira cheke cha ndalama zoti amangire nyumba za aphunzitsi komanso kukonza sukulu yawo kumeneko zomwe wati ndichitsimikizo kuti zinthu zikuyenda. Iye wati umbava ndi umbanda wakula kudera lake kotero boma likuyenera kuchita kanthu. Mfumu yaikulu Malemia ya mboma la Nsanje yati zinthu zili bwino mmidzi chifukwa boma lati liyambitsa ntchito zachitukuko mmidzi zomwe wati zitukula anthu akumudzi. Addition Mawononga wa mmudzi mwa Matiya kwa T/A Nkumbira mboma la Zomba wati boma likhwimitse chitetezo. Chitetezo chacheperatu, Lamulungu pa 15 akuba adandibera K10 000 ndipo siine ndekha anthu akulira mdziko muno. Komanso tikumva kuti mkulu wa apolisi mdziko muno Lot Dzonzi wauza apolisi kuti asamawombere akuba; izi sizonena kulankhula pagulu, bwezi atangowauza apolisiwo koma momwe ateremu ndiye kuti chitetezo chimasukiratu, adatero mkuluyu. ",11 " Achinyamata akambirana za mmanifesto Nthambi ya achinyamata ya chipani cha Malawi Congress Party (MCP) yakambirana mfundo zokhudza achinyamata zomwe chipani chawo chiyike mmanifesto yake yokopera anthu pachisankho chikudzachi. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Woyanganira za achinyamata Richard Chimwendo Banda watsimikiza izi ndipo mneneri wachipanichi mbusa Maurice Munthali wati kupatula achinyamatawa, chipanichi chikulandira maganizo kuchokera ku magulu osiyanasiyana. Ena mwa achinyamata amene adafika kumsonkhanowo Tili mkati mopanga manifesto yathu poonjezera zomwe tidaiwala mu 2014. Imodzi mwa nthambi zomwe taikapo mtima kwambiri ndi achinyamata tsono tidaona kuti nkwabwino akambirane okha mfundo zowakhudza nkutipatsa, watero Munthali. Achinyamata a MCP a mchigawo chapakati ndi nthumwi za mzigawo zina amakumana kulikulu la chipanichi pa 23 ndi 24 August mumzinda wa Lilongwe kukambirana mfundozo ndipo Chimwendo Banda wati msonkhano ngati omwewu ukachitikaso mzigawo zina. Pamsonkhanowu, tidali ndi achinyamata 1 000 ochokera mmadera onse oyimiliridwa ndi aphungu mchigawo chapakati ndi mphepepete mwanyanja komanso nthumwi za mmakomiti a mzigawo. Misonkhano ngati yomweyi ikachitikanso mzigawo zina, adatero iye. Iye adati kumsonkhanoko, achinyamata adatulutsa nkhani zambiri zowakhudza nkuzikambirana ndipo adamanga mfundo za momwe akuonera kuti nkhanizi zikhonza kukonzedwa ndi atsogoleri. Iye wati chipanichi chidachita izi ngati njira imodzi yoperekera mphamvu kwa achinyamata kupanga ziganizo za momwe dziko lingayendere bwino ndipo wati ali nchikhulupiriro kuti atsogoleri a chipanichi akhutitsidwa ndi mfundozo. Pothirirapo ndemanga, Munthali adati komiti yaikulu idasangalala koposa ndi momwe msonkhano wa achinyamatawo udayendera komanso mfundo zomwe adamanga nkupereka ku likulu. Mfundo zomwe adatipatsa zikusonyeza kuti mchipanimu tili ndi achinyamata akupsa mmaganizo omwe angathandizedi pachitukuko cha dziko. Mfundo zawo tazitenga ndipo tiziphatikiza mmanifesto yathu chifukwa nzokomera achimata onse mdziko muno, watero Munthali. Woyendetsa gulu la mphala ya achinyamata la Youth Consultative Forum Edward Chileka Banda wayamikira zomwe chipani cha MCP chapanga ndipo wati zingakhale bwino zipani zonse zitatengera mchitidwewu. Zimenezi nzomwe timafuna ngati achinyamata kupatsidwa mphamvu osati kumangogwiritsidwa ntchito ngati osapota chipani kapena zida za zipolowe ndi andale ayi. Uku ndiye kuphunzitsa achinyamata utsogoleri, watero Chileka Banda. Iye wati kupatula momwe chipani cha MCP chapangira, mpofunikaso kuti achinyamata azipatsidwa mpata wokwanira ogwira ntchito zogwirizana ndi maluso awo osati kumangowaponderedza. ",11 "Kulandira Mawu a Mulungu ndi Kulandira Yesu-Papa Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wati povomera kulandira mawu a Mulungu akhristu amalandira Yesu Khristu yemwe. Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican, Papa walankhula izi lamulungu ku likulu la mpingowu ku Vatican. Iye wati fanizo la wofetsa mbewu ndi lothandiza akhristu kuwunika za moyo wawo maka umo mmene alandilira mau a Mulungu. Mu zolankhulalankhula zake pa tsiku lamulungu la 15 mu nyengo ya pa chaka Papa Francisco wafotokozera Uthenga Wabwino womwe unawerengedwa pa tsikuli omwe ndi fanizo la wofetsa mbewu. Iye wati sikungakhale kulakwitsa kunena kuti fanizo la wofetsa mbewu ndi manthu wa mafanizo opezeka mu Baibulo popeza ili ndi fanizo lomwe likunena mwa mvemvemve zakufunika komvetsera Mau a Mulungu. Papayu wapitiriza kunena kuti Mau a Mulungu ndiye Yesu Khristu kotero amene amvetsera ndikuvomera Mau a Mulungu ndiye kuti akuvomera ndi kulandira Yesu Khristu amene. Iye wati Mau a Mulungu omwe ndi mbewu mu fanizoli ndi Yesu Khristu amene ndi Mau a Mulungu odzipangidwa munthu. Papa Francisco wati akhristu akuyenera kulandira Mau a Mulungu monga nthaka yabwino yomwe ichititsa mbewu kumera, kukula mpaka kubereka zipatso. Iye wati Mawu a Mulungu ali ngati mbewu imene Mulungu amafetsa pakati pa anthu ake. Papa Francisco wati munthu aliyense ali ngati nthaka pomwe mbewu yomwe ndi Mau a Mulungu amagwerapo ndipo kuti zili kwa munthu aliyense kusankha kuti akhala nthaka yotani. Ichi ndi chisankho chomwe munthu aliyense akuyenera kuchita pa moyo wake wa chikhristu. ",13 "Msusa Alimbikitsa Akhristu Kulemekeza Masacrament Wolemba Richard Makombe w/wp-content/uploads/2019/09/msusa.jpg"" alt="""" width=""310"" height=""263"" />Msusa: Mabanja sakuchedwa kutha Akibishop Thomas Luke Msusa wa akidayosizi ya Blantyre wapempha akhristu kuti akhale okonda kusunga ma sacrament. Akibishop Msusa amayankhula izi lamulungu pa mwambo wa chibalalaitso cha mpingo omwe unachitikira ku St. Pius Parish mu akidayosizi ya Blanytre . Bishop Msusa wati nkofunika kuti akhristu akhale olemekeza komanso kusunga bwino ma sacrament makamaka sacrament la ukwati. Ndizodandaulitsa kuona kuti tikadalitsa ukwati koma pakangotha chaka chimodzi uona kuti ukwati uja watha, choncho sibwino, anatero bishop Msusa. Bishop Msusa anatengerapo anathokoza parish ya St Pius kamba kokhala parish ya chitsanzo povomera kuchititsa mwambo wa chaka achino wa chaka cha chibalalitso. Ndithokoze akhristu komanso ansembe onse popemphelera mwambowu kuti ukhale opambana, anatero Akibishop Msusa. Chaka ndi chaka mpingo wa katolika umachititsa mwambo wa chibalalitso cha mpingo omwe cholinga chake ndikufunakupeza thandizo la ndalama zothandizira kukulitsa mpingowu pa dziko lonse. ",13 " Ndalama zakale zitha pa 23 May Banki yaikulu yakumbutsa mabanki a mdziko muno kuti ndalama zakale za Chilembwe dziko lino zisiya kugwira ntchito pa 22 May. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mchikalata chimene mkulu wa bankiyo Mary Nkosi adalembera mabanki a mdziko lino, bankiyo idalengeza pomwe limakhazikitsa ndalama zatsopanozo pa 23 May chaka chatha kuti pofika pa 22 May, ndalama zakale zikhala zitasiya kugwira ntchito. Koma ngakhale ndalama zapepala zisiye kugwira ntchito patsikulo, ndalama zachitsulo zidzakhala zikugwira ntchito mpaka mtsogolo muno, adatero Nkosi. Mchikalatacho, Nkosi adapempha mabanki kuti asamapereke ndalama zakalezi kwa makasitomala awo. Mabanki ayenera kutenga ndalama zakalezo ndi kukazisiya ku Reserve Bank akazilandira. Chenjezo kwa mabanki ndilakuti ayenera kusamala ndi ndalama zachinyengo, adatero Nkosi. Ambiri ati Chilembwe ngakhale idali khobili lokongola tsamba lake lidali lalikulu kotero simakwana bwino mu matumba komanso mzikwama zosungila ndalama poyenda (waleti). ",2 " Chenjerani pokolola Mbewu ya chimanga nayo imafuna kuyichengetera nthawi yokolola kuti zokolola zikhale zochuluka ndi zopatsa kaso. Wachiwiri kwa mkulu woona za kafukufuku wa mbewu ku Bvumbwe Research Station, Frank Kaulembe akuti nankafumbwe amaononga ngati alimi akolola chimanga chawo mochedwa kapena mofulumira. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Namkafumbwe amachecheta mosavuta chimanga chokololedwa mofulumira Mwachitsanzo, iye adati kukolola mbewuyi isadaume, mlimi akaiyanika imafota ndipo zotsatira zake nankafumbwe amaboola mosavuta. Mlimi akaichedwera, nankafumbwe wamkulu amayamba kuionongera kumunda komweko, iye adatero. Iye adaonjeza kuti kukolola chimanga chosauma nthawi yoyanika chimakumana ndi ndi mavuto monga kunyowa ndi mvula yowaza komanso kukachita chifunga mmawa, chimayamwa chinyontho mapeto ake chimachita chukwu, iye adatero. Pothirirapo ndemanga pa zomwe adayankhula Kaulembe, Paul Fatch, mphunzitsi wa kunthambi ya za ulangizi ya ku Lilongwe University of Agriculture and Natural Resources (Luanar), adati chimanga chimayenera kukololedwa chikakhwima komanso kuuma bwino ndipo chizindikiro chake nchoti chimaloza pansi. Pomwe, chimanga chimakhala chaumiratu ndipo kutonola chochepa ndi kuchiponya pansi chimachita phokoso, iye adatero. Ngakhale izi zili chomwechi, Fatch adati madera ena amayenera akololebe mwachangu kuopetsa akuba, chiswe komanso makoswe kotero alimi oterewa amayenera akachiumitse akafika nacho kunyumba pogwiritsa ntchito nkhokwe zoumitsira kapena dzuwa. Kaulembe adafotoza kuti mlimi sakuyenera kulowa mmunda ndi kuyamba kukolola chimanga tsiku lomwe kwachita mitambo ndipo kukuonetsa kuti nthawi ina iliyonse kukhoza kugwa mvula. Iye adati chimanga chikanyowa ndi mvula chimachita chukwu. Kaulembe adati ngati nthawi yokolola yafika koma kunja kukugwabe mvula, mlimi ayenera kuthandizira chimanga chomwe sichidaloze pansi kuti chitero ndi cholinga choti madzi asalowe mchimanga muja koma azingotsetsereka kufikira ataona kuti mvula yaleka. Ichi nchifukwa chake kale makolo ankasanja chimanga chawo mnkhokwe molozetsa pansi kotero ngakhale mugwere mvula, sichimaonongeka, iye adatero. Kuonjezera pa nankafumbwe yamwe amatha kuyamba kuononga chimanga chikakhalitsa mmunda,Kaulembe adati alimi asamakolole mochedwa kwambiri kuopetsa chiswe ndi moto olusa. Pokolola, mlimi aziona pomwe akuika chimanga chake chifukwa chikakhala pafupi ndi chulu, chimagwidwa ndi chiswe komanso akaika pachidikha, chinyontho chimaononga, iye adatero. Mlimi wa chimanga mboma la Salima Matiyasi Banda adati saphuphulumira kukolola chimanga chake chifukwa amafuna kuti chiumiretu, akangofikira kutonola, kuthira mankhwala ndi kuchisunga. Ndidaona kuti kuyanika ndi ntchito ina yolemetsa yapadera kotero ndimangochisiya mmunda momwemo kuti chiumiretu. Ndimakolola pokhapokha makoko ake akamaoneka ouma kwambiri, iye adatero. Mlimi wina wa mboma la Lilongwe Dust Chikumbutso adati amakolola mwamsanga kuopetsa akuba. ",4 "Bambo Anjatidwa Kamba Kogwililira Gogo wa Zaka 75 Apolisi mboma la Chikwawa amanga bambo wina wa zaka 27, pomuganizira kuti wagwililira gogo wa zaka 75 pamalo ena omwera mowa mbomalo. Malinga ndi wachiwiri kwa wofalitsa nkhani za apolisi mbomalo Sergeant Dickson Matemba, mkuluyu Yesani Chumachawo, anapalamula mlanduwu usiku wa pa 31 May 2020, pomwe iye ndi gogoyu anali limodzi pa malo ena omwera mowa. Gogoyu atanyamuka pa malowa kubwelera kwawo, mkuluyu akuti anamutsatira, atafika kutali ndi anthu, mkuluyu anakokera gogoyu pa tchire ndi kuchita naye zadama. Ndizoona tatsekera mchitokosi bambo wina wa zaka 27 yemwe anagwililira agogo wazaka 75 usiku wina mchaka chino cha 2020, anatero Sergeant Matemba. Mwapadera apilosi ayamikira a chitetezo chakumidzi kaamba kothandizana ndi apolisiwa kupeza mkuluyu yemwe anathawa atachita izi. Padakalipano mkuluy akuyembekezeka kukawonekera ku bwalo la milandu posachedwapa kuti akayankhe mlanduwu. ",7 " Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Bungwe la Human Rights Defenders Coalition (HRDC) lati maso ake akadali otsegula ncholinga choti boma la Tonse Alliance lisaphwanye ufulu wa Amalawi. Mkulu wa bungweli Gift Trapence wauza Tamvani kuti HRDC iwonetsetsa kuti mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera wakwaniritsa zomwe adalonjeza Lolemba kuti achepetsa mphamvu zake. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Trapence: Maso adakali otsegula Chakwera adapereka lonjezolo pamwambo wokondwerera kuti dziko la Malawi latha zaka 56 lili pa ufulu wodzilamulira. Mtsogoleriyu adalonjezanso kuti azipita ku Nyumba ya Malamulo kukayankha mafunso okhudza momwe akuyendetsera dziko lino. Chakwera adati awonetsetsanso kuti lamulo loti anthu akupeza mauthenga a boma mosavuta (Access to Information) layamba kugwira ntchito ncholinga cholimbikitsa kuchita zinthu poyera, komanso kuchepetsa ziphuphu ndi katangale. Adalonjeza kuti achotsa mphamvu zina za Pulezidenti ndipo mphamvu zimenezi zikhudze ku nthambi ya zachitetezo. Pulezidenti akakhala ndi mphamvu zambiri, nthambi ya chitetezo imasanduka ngati yake osati ya dziko, adatero Trapence. Iye adapempha Chakwera kuti awonetsetse ku mboma lake mulibe katangale ndi ziphuphu. Mphekesera za katangale zifufuzidwe ndipo mutu wake uzioneka, iye adatero. ",11 "CMO Iyamikra Abambo a Parish ya Mwanza es=""(max-width: 564px) 100vw, 564px"" />Abambo a Mwanza parishi kujambulitsa limodzi ndi abambo a ku Nthawira parishi Bungwe la Umodzi wa Abambo la Catholic Men Organisation (CMO) mu arkdayosizi ya Blantyre layamikira abambo a chikatolika a mparishi ya Mwanza ya mpingowu kamba kobwera mwaunyinji ndi kuzamvera mfundo, zolinga ndiponso masomphenya a bungweli Mkulu wa bungweli mu arkdayosizi ya Blantyre a Martin Chiwaya alankhula izi ku parishiyi lamulungu pa 1 December, 2019 pokhazikitsa bungweli ku parishiyi. Iwo ati akhutira ndi momwe abambo a mparishiyi mmene anatulukira ku zamvera mfundo zothandizira kupititsa patsogolo ntchito za bungwe latsopanoli Abambo aku Mwanza bungweli alirandira kwambiri, taona kuti abambo ambiri ochokera mmatchalitchi omwe ali pansi pa parishiyi anatsalira kuti amve zolinga za bungweli,anatero a Chiwaya Pamenepa iwo ati zoterezi zithandiza abambo a mu mpingowu kugwira nawo ntchito za mumpingo mmalo mosiyira amayi okha. A Dausi kufunsa mafunso pa zolinga za bungwelo Chidwi chomwe abambo akuchionetsa zikutilimbikitsa kwambiri kuti tsopano abambo ayamba kutulikira poyera ndi kukhala patsogolo pothandiza mpingo, anapitiliza a Chiwaya. Mau ake mmodzi mwa abambo a mparishiyi wolemekezeka a Nicholas Dausi omwenso ndi nduna ya boma komanso phungu waderali anati kubwera kwa bungweli kuthandizira abambo a mparishiyi kukhala pamodzi ndi kukweza miyambo ya chipembedzo komanso zochitika mu mpingo. Pamenepa a Dausi alimbikitsa abambo onse achikatolika kulowa nawo mbungweli mmaparishi awo Talimbikitsa kuti abambo ambiri tilowe mu bungweli kuti potero tizithandizana, tizizuzulana komanso tizizutsana wina mwa ife akagwa kuti mapeto ake tonse tikalowe mu ufumu wa Mulungu anatero a Dausi. Bungwe la Umodzi wa abambo mu arkdayosizi ya Blantyre likupitilizabe kuyendera maparish osiyanasiyana ndi cholinga choti lifikire mmaparish onse 43 amu arkdayosiziyi. Lamulungu la pa 8 December, 2019 bungweli kudzera mmakomiti okhazikika a mmaparishi ena ayendera ndikukhazikitsa bungweli mmaparishi za Lunzu, Mkhwayi, Nyungwe komanso Thunga. ",13 "Amangidwa Kamba Kogwilira Msungwana Ozelezeka Apolisi mboma la Chikwawa akusunga mchitokosi bambo wina wa zaka 35 zakubadwa Charles Mikeyasi kamba komuganizira kuti wagwilira mtsikana wa zaka 18 zakubadwa yemwe ndi wozelezeka. Malinga ndi wachiwiri kwa mneneri wa apolisi mbomali Sergeant Dickson Matemba, izi zachitika pa 18 mwezi uno, pomwe bamboyu yemwe amachokera ku mowa anakumana ndi msungwanayu pomwe anamukokera pa tchire lina la kufupi ndi komwe mtsikanayu amachokera ndi kumugwilira. Anthu ozungulira ndi omwe anagwira bamboyu ndi kukamutula mmanja mwa apolisi. Ndizoonadi kuti apolisi kuno ku Chikwawa tamanga bambo wina yemwe wagwirira mzimayi wa zaka 18 yemwe ali ndi ulumali wa mu ubongo pamene amachokera ku mowa, anatero Sergeant Matemba. Iwo ati bamboyu akawonekera ku bwalo la milandu posachedwa ndipo pakadali pano apolisi achenjeza anthu ku derali kuti adzisamalira ana awo omwe ali ndi ma ulumali onga awa pomayenda nawo limodzi. A Charles Mikeyasi amachokera mmudzi mwa bwalo mfumu yaikulu Kasisi mboma la Chikwawa. ",7 "Chipembedzo cha Chisilamu Chayamikira Kalata ya Maepiskopi Bungwe lowona za ufulu wa anthu ku chipembezo cha chisilamu la Muslim Forum for Democracy and Peace, layamikira chikalata maepiskopi a mpingo wa katolika mdziko muno alemba momwe alankhulapo pa momwe zinthu zikuyendela mdziko muno. Kawinga ndi akuluakulu ena a bungwe la MFDP Mkulu wa bungweli Sheikh Jafah Kawinga wauza Radio Maria Malawi kuti ndi udindo wa mpingo kulankhulapo pa momwe zinthu zikuyenera kuyendera komanso momwe mzika zikuyenera kuchitira pofuna kukweza dziko lino. Sheikh Kawinga ati munthu ndi thupi ndi mzimu pamodzi choncho ndi koyenera kuti pamene mpingo ukupereka chiwuniko cha uzimu, pomweponso mpingo upereke zofunika ku thupi. Mpingo ukuyenera kulankhulapo pamene zikuchita bwino komanso pamene zisakuchita bwino chifukwa ukakhala chete ndiye kuti ukugwirizana ndi zomwe zikuchitikazo, anatero Sheikh Kawinga. Iwo adzudzulanso anthu ena omwe amanena kuti mpingo wa katolika ukulowelera ndale ponena kuti anthuwo sadziwa mbiri ya zipembedzo kaamba koti ati zimenezi zimachokera mu baibulo komans Quaran. ",13 " anatchezera Akuti tibwererane Anatchereza, Ndinali pambanja ndi mwamuna wa ku Nsanje ndipo ndili naye mwana mmodzi. Koma ndikati tiyeni tikaone kwanu amangoti tidzapitabe chikhalireni palibe ndi tsiku ndi limodzi lomwe abale ake anabwerapo pakhomo pathu ndiponso banja lathu ndi losagwirizira chinkhoswe. Kumudzi kwathu mwanuna wangayu amakananso kukaonako. Panopa tinasiyana chifukwa samagona mnyumba. Mowa samwa komanso fodya sasuta. Ndiye panopa akukakamira kuti tibwererane, apo bii ndimupatse mwana wake, koma ineyo ndikukana. Gogo, ndithandizeni. Nditani pamenepa? Mwati mudali pabanja, koma banja lanu padalibe chinkhoswe? Ndiye lidaali banja lotani lodziwa awiri nokhanu? Apa mukuchita kudabwa kuti a kwawo kwa mwamuna wanu sadabwerepo pakhomo panu ngakhale tsiku limodziakadabwerapo bwanji ngati akukudziwani? Munasiyana koma pano mwati akukakamira kuti mubwererane, pachifukwa chiti? Mwachidule, ndinene kuti mmphechepeche mwa njovu sapita kawiri. Kubwererana ndi mwamuna wotere kuli ngati galu kubwerera kumasanzi akepalibe chanzeru. Koma ngati watsimikiza kuti amakukonda ndipo nawenso umamukondabe, ulendo uno muyesetse kuti akwawo ndi akwanu akumane ndi kukambirana kuti pakhale dongosolo lenileni, chinkhoswe kenaka ukwati wovomerezeka ndi mbali zonsezonse. Pokhapo ndiye kuti mutha kumanga banja, osati zachibwana zimene mudachita kupatsana mwana kenaka wina aziti tibwererane apo bii undipatse mwana wanga. Banja si masanje, chonde! Zikomo, Natchereza Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Akuthawathawa Anatchereza, Mwezi wa April 2011 ndinapeza mwamuna ndipo sindinagonane naye kufikira 6 July 2012 pamene tinakaonekera kwa makolo a tonse. Tsiku limneli andiuza kuti tigonane koma ndinawauza kuti tikayezetse kaye HIV koma adakana ponena kuti iwo ndi blood donor choncho ndisawakaikire ndipo zinatheka. Titasiyana tsiku limenelo adandiuza kuti tikadziwe komwe amagwira ntchito ku Zomba. Nditapita andiuza kuti ndisabwererenso tiyambiretu banja koma ndinakana ndipo ndidabwerera. Patapita masiku adabwera ndi amalume awo kudzafunsira mbeta ndipo zinatheka. Pambuyo pake tidayamba banja ndipo posakhalitsa ndidaima. Mwanunayu adandiuza kuti mmamawa azidya phala ndipo nsima izikhala ya mgaiwa. Chodabwitsa chinali choti phala likafika patebulo limasintha mtundu kukhala lobiriwira (green) koma kuwafunsa samandiyankha zomveka. Nditalimbikira anandionetsa mabotolo awiri momwe munali zinthu za ufa za green koma anakana kundiuza ntchito yake, ati sizimandikhudza. Tsiku lina ananditenga kuti tikayezetse magazi koma titafika kumneko anandiyeza ndekha ati iwo adyezetsa kale. Anandipeza ndi kachilombo ka HIV. Kuyambira tsiku lomwelo anandiuza kuti banja latha ndizipita kwathu. Ndinakatula nkhaniyi kwa amalume awo koma palibe chikuchitika. Nditani? M Zikomo M, Sindidziwa kuti kachilombo ka HIV mudatatenga bwanji, koma sindikukaika kuti mwamuna wanuyo ndi amene adakupatsirani kachilomboko ndipo zikuonetseratu kuti amachita izi uku akudziwa kuti ali ndi HIV. Ndatero chifukwa cha zochita zakeakuonekeratu kuti alibe chilungamo mzochitika zake. Nanga timabotolo ta mankhwala obiriwira amathira mphalato ntachiyani? Nanga amakana kukayezetsa chifukwa ninji? Pano inu mwapezeka ndi HIV akuti banja latha, zoona? Ndithu, ngati iyeyo adali walungalunga, akadatha kuchitapo china chake kuonetsa kuti wakhumudwa kuti inuyo ndi amene mwamupatsira kachilomboko. Pali malamulo mdziko muno, oti wina akapatsira mnzake kachilombo ka HIV mwadala, ameneyo ali ndi mlandu. Ndithu, pitani nayoni nkhaniyi kwa odziwa malamulo kuti akuthandizeni. ",12 " Kuthana ndi vuto Kwa zaka 20, gulu la alimi a ngombe za mkaka la Namahoya la mboma la Thyolo silimapeza phindu mnyengo ya mvula chifukwa limangogulitsa mkaka wokwana magawo 10 pa 100 aliwonse nthawi zina osagulitsa ndikomwe. Wapampando wa gulili Taulo Chisoso adati izi zimachitika chifukwa ogula akayeza mkaka umaupeza uli ndi madzi wochuluka. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Wyson kudyetsera udzu ngombe yake Koma padakali pano, mkuluyu adati vutoli adathana nalo. Kwa zaka zonsezi, nyengo ya mvula ikafika kwambiri tinkangodyetsera udzu wauwisi chifukwa umapezeka wochuluka osadziwa kuti tikuzionongera msika, adatero Chisoso yemwe gulu lake lili ndi mamembala 550. Mu 2016 tidapeza ulangizi woti kudyetsera kwambiri ngombe za mkaka msipu wobiriwira, kumachulukitsa madzi ku mkaka ndipo titaleka, taona kuti chaka chonse chatha mpaka lero sudabwererepo pamsika, adatero Chisoso. Mlimiyu adati kampani yomwe imawagula, imafuna mkaka wabatala loyambira magawo 20 pa 100 aliwonse. Akalephera kukwaniritsa izi, amaubweza. Membala wa gululi, Chrissie Wyton, adati mmbuyomu nyengo ya mvula ikafika amadyesera msipu wauwisi wabwiri chifukwa deya amakwera mtengo, komanso samapanga mfutso wa ziweto. Padakali pano, ndidaleka kudyetsera udzu wauwisi wochuluka chifukwa ndimapanga mfutso pophatikiza msipu wa mitundu yosiyanasiyana kuti zikamadya, zizipeza michere yokwanira mthupi. Kuonjezera apa, ndimasunga madeya chifukwa ndazindikira kuti ulimiwu ndi bizinesi choncho ndikuyenera kumaikirapo mtima, iye adatero. Mlangizi wa ziweto ku Mzuzu Agriculture Development Division (Mzaad), Jacob Mwasinga, adafotokoza kuti kudyetsera kwambiri ngombe za mkaka msipu wa uwisi kumakhala ngati mlimi akuzipatsa madzi ambiri, koma chakudya chochepa. Izi zili chomwechi chifukwa msipuwu, umangochuluka madzi, koma michere imachepa. Mkaka umakhala wochuluka, koma ngakhale kungouyangana, umaoneka ngati wathiridwa madzi choncho sungayembekezere zabwino pamsika, iye adatero. Mwasinga adafotokoza kuti udzu umakhala ndi michere yochulukirapo mapeto a mwezi wa February kapena mayambiriro March. Iye adati izi zili chomwechi chifukwa umakhala wakula ndipo ukupita kokhwima kotero umakhala ndi michere yochulukirapo. Mlangiziyu adati ichi nchifukwa chake alimi amayenera kupanga mfutso wa ziweto udzu ukafika pamenepa. Pothirirapo ndemanga, mphunzitsi wa ziweto wa ku Lilongwe University of Agriculture and Natural Resources (Luanar), Jonathan Tanganyika, adati ngakhale msipu ndi wodalirika pa ulimi wa ziweto, alimi azichulutsa chakudya choonjezera mu nyengo ya mvula. ",4 " 2018: Chaka cha ululu Mu February 2018, Dorothy KampaniNyirenda amagwiritsira magetsi a K2 500 pa mwezi. Kufika mu October mpaka lero, Nyirenda akugwiritsira magetsi a K5 000 pa mwezi. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kukwera mtengo wa mafuta kudaliza Amalawi Mayiyo amene amakhala ku Bangwe mumzinda wa Blantyre, adati mu February, 2018 amagwiritsira ntchito K700 kulipirira minibasi kuti akafike ku Trade Fair komwe amapanga bizinesi. Lero zasintha pamene akugwiritsira K1 000 mtunda womwewo. Uwu ndiye ululu umene anthu akhala akuumva mchaka cha 2018 kutsatira kukwera mtengo kwa mafuta agalimoto komanso kukwera kwa magetsi komwe kudapangitsa kuti zinthu zikwerenso. Malinga ndi malipoti a Centre for Social Concern (CfSC), banja la anthu 6 mchaka cha 2017, limafunikira likhale ndi K183 000 pa mwezi. Izi zimachitika pamene ndalama yotsikitsitsa yomwe munthu amalandira idali pa K19 000. Koma mu 2018, banja la anthu 6 limayenera likhale ndi K190 549 pa mwezi pamene ndalama yotsikitsitsa yomwe munthu amalandira idali pa K25 000. Kutanthauza kuti banja la anthu 6 okhala mtauni amalowa mmasautso osaneneka kuti athe mwezi umodzi chifukwa zomwe amapeza zimasiyana ndi zomwe zimafunikira. Magetsi akhale akukwera mchakachi. Pamene timamaliza 2017 nkuti mafuta a petulo akugulitsidwa K888 00 pa lita imodzi ndipo dizilo adali pa K890 90 pa lita imodzi. Mafutawo adakwera kanayi mchakachi ndipo petulo adafika pa K990 50 pamene dizilo adafika pa K990 40 pa lita. Izi zidachititsa kuti maulendo a minibasi akwere ndi 5 pelesenti mdziko muno. Mu October, bungwe logulitsa magetsi la ESCOM lidakweza magetsi ndi ndi 31.8 pelesenti. Kwa amene amagwiritsira magetsi a K7 714 pa mwezi adayamba kugwiritsira ntchito K10 105 pa mwezi. Zinthu zambiri zofunikira pamoyo wa munthu zidakwera mtengo monga thumba la chimanga lolemera ndi makilogalamu 50 lidafika pa K10 000 kuchoka pa K5 000 mu June mchakacho. Kwa KampaniNyirenda, chakachi chidali chowawa chifukwa mitengo ya zinthu zidakhazikike. Vuto lalikulunso nkuti bizinesi simayenda ndiye kuti upeze ndalama yogulira chakudya pakhomo ndi yoyendera kwakhala kovuta, adatero. Mkulu wa bungwe loona za anthu ogula la Consumer Association of Malawi (Cama), John Kapito adati ngakhale mchakachi ndalama ya kwacha idaoneka kuti idali ndi mphamvu, komebe izi sizidathandize ogula. Anthu akuvutika kuti agule katundu, nthawi iliyonse mitengo ikungosintha. Boma likuyenera libweretse yankho kuti chaka chino anthu asavutike, adatero. Kapito adati chaka cha 2019 chingakhale chabwino kwa anthu ngati boma litaonetsetsa kuti mitengo ya zinthu zofunikira kwambiri pamoyo wa munthu sizikukwera mwachisawawa. ",2 " Zampira zenizeni ndi CJ Banda John CJ Banda ndi kaputeni wa Blue Eagles, komanso ndi katundu wofunika ku Flames. Iye wapeza mwayi wokasewera ku Jomo Cosmos mdziko la South Africa. Kodi apita liti? Nanga mbiri yake ndi yotani? BOBBY KABANGO akucheza naye. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Dzina lonse ndi ndani? Banda: Amanditcha CJ Dzina langa ndi John Banda koma ondikonda amati John CJ Banda. Okukonda ake ati? Nanga CJ akutanthauzanji? Anthu a kwathu ku Nkhata Bay ndiwo adandipatsa dzina la CJ, chidule cha Christopher John Banda amene ankasewera mu Big Bullets. Ati timasewera mpira wofanana. Ena amaganiza kuti adali bambo anga koma ayi, padalibenso chibale ndi ine. Tamva kuti ukupita ku South Africa, unyamuka liti? Ulendo mwina ulipo kapenanso ayi. Izi zili chonchi chifukwa eni akewo adamaliza nambala ya osewera akunja amene amayenera alembe komanso nkhani yeniyeni yomwe ndikudziwa ine ndi yakuti sadamalize kupereka ndalama kutimu yanga yomwe adagulira Micium Mhone. Koma zonse zikatheka ndiye mu May muno tipitako komanso dziwani kuti pali matimu ena amene akundifuna ngakhale matimuwo sindingawatchule maina awo pano. Koma mayeso mudakhozadi? Kwambiri, ngakhale mutafunsa eni timu akuuzani kuti zidatheka, ntchito tidagwira. Tandiuzako za chiyambi chako pa chikopa. Ndidayamba kusewera mpira ku Eagle Strikers mu 2008. Tidali osewera amene tidailowetsa muligi ndipo idatha chaka osatuluka. Mu 2010 ndidachokako ulendo ku Police Training School. Kuchoka uko ndi pomwe ndimadzayamba kusewera mu Blue Eagles. Tidawina Standard Bank Cup mu 2011, Carlsberg Cup mu 2012 ndi Fama Cup mu 2012. Nanga mbiri yako ku Flames? Ndidatengedwa kukasewerera Flames mu 2011 pamene timamenya ndi Kenya. Ndasewera magemu 46 ndipo ndachinya zigoli 10, chaka chathachi ndidachinya zigoli zinayi kuposa osewera aliyense mu Flames. Koma ndimasewera pakati. Uli pabanja? Mkazi uyo akumvayo, dzina lake Jane komanso mwana alipo dzina lake Sean. Kodi udindo wako ndi wotani ku polisiko? Ndine Inspector kulikulu la polisi ku Area 30. ",16 " Kalembera wafika kummwera Kalembera wa mkaundula wachisankho cha chaka cha mawa wafika mchigawo cha kummwera tsopano ntchitoyi itakumana ndi zokhoma zosiyanasiyana mmaboma a mchigawo chapakati pomwe idayambirira. Boma la Ntcheu ndi boma lomaliza la mchigawo chapakati komwe kwafika kalemberayu mgawo lachinayi ndipo mgawo lomweli muli maboma a mchigawo cha kummwera monga a Blantyre, Mwanza ndi Chikwawa. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Ntchito ya kalembera Kalemberayo adayamba Lachinayi ndipo adzatha pa 29 August. Malingana ndi mkulu woyanganira zisankho ku Malawi Electoral Commission (MEC), Sam Alfandika, pali chiyembekezo choti pamene ntchitoyi ikupitirira, mavuto omwe amaoneka mmagawo atatu oyambirira achepa kwambiri chifukwa anthu aphunzira mokwanira za kalemberayu. Kumayambiriro kuja tidali ndi vuto loti anthu ambiri adali asadadziwitsitse za kalemberayu koma pano ndi mauthenga omwe akhala akuperekedwa, anthu ambiri akudziwa ndipo chiyembekezo nchachikulu kuti ziyenda bwino, adatero Alfandika. Iye adapempha kuti zipani zitengepo mbali yaikulu yomema anthu kuti akalembetse chifukwa anthu omwewo ndiwo mavoti awo. Mkulu wa bungwe lophunzitsa anthu la National Initiative for Civic Education (Nice) Trust, Ollen Mwalubunju wati bungwelo lipitiriza kuphunzitsa anthu mmadera momwe mukulowera kalemberayu kuti cholinga chenicheni cha demokalase chidzawoneke pachisankho cha chaka chamawa. Zimakhala zofoola nkhongono kuona kuti anthu ochepa ndiwo avota kusankha atsogoleri chifukwa zimakhala ngati ena aja angokakamizidwa kutsogoleredwa ndi anthu omwe sadawafune, ndiye tikufuna ulendo uno, aliyense yemwe ndi woyenera kuvota akavote. Chiyambi cha zonse ndi kulembetsa, adatero Mwalubunju. Iye adati ndi wokondwa ndi momwe kalembera adayendera mgawo lachitatu lomwe limachitika ku Lilongwe ndipo adati izi zidatheka chifukwa bungwelo ndi mabungwe ena komanso mipingo ndi zipani adagwirana manja kumema anthu. Poyamba kalemberayu mmaboma a Kasungu, Salima ndi Dedza, padali mavuto aakulu okhudza kufaifa kwa zipangizo mpakana anthu ambiri sadalembetse. Mavutowa adapitirira mgawo lachiwiri ku Mchinji, Dowa, Ntchisi ndi Nkhotakota moti chipani cha Malawi Congress (MCP) ndi mabungwe ena monga la Centre for Human Rights and Rehabilitation (CHRR) adapempha MEC kuti idzabwereze kalembera mmabomawa. Mavutowa adadzachepa mgawo lachitatu lidatha sabata yatha koma padapezeka mavuto ena monga anthu kulandidwa ziphaso komanso miyambo yamakolo yomwe imabwezera kalembera mmbuyo. ",11 " Mavuto a madzi akula mu October ku Lilongwe Pomwe anthu mumzinda wa Lilongwe akubangula ndi vuto la kuzimazima kwa magetsi, kampani yopereka madzi ya Lilongwe Water Board yachenjeza kuti madzi nawo avuta mwezi ukudzawu. Mneneri wa bungweli, Bright Sonani, watsimikiza za nkhaniyi koma wati anthu asade nkhawa kwambiri chifukwa madzi azitulukabe ngakhale mwa apo ndi apo. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Sonani wati bungweli litulutsa ndondomeko ya mmene madzi azitulukira kuti anthu azitunga nkusunga madzi okwanira mmakomo mwawo panthawiyi. Mwezi umenewu tikhala tikukonza ena mwa mathanki omwe timasungiramo madzi. Tikuchita izi malingana ndi kuti anthu ogwiritsa ntchito madzi akuchuluka ndiye tikufuna kukhala ndi mosungira mokwanira, adatero Sonani. Malingana ndi chikalata chomwe bungweli lasindikiza, madzi azidzasiya 6 koloko mmawa ndi kuyambanso kutuluka 6 koloko madzulo ndipo tsiku loyamba kusiya ndi Lolemba pa 28 September. Potsirapo ndemanga, wapampando wa mabungwe a anthu ogwiritsa ntchito madzi mumzinda wa Lilongwe, Bentry Nkhata, wati nkhaniyi ndi yoopsa polingalira kuti anthu amadalira madzi pamoyo wawo wa tsiku ndi tsiku. Iye adati madzi akasowa matenda, makamaka ammimba monga kolera ndi kamwazi, amabuka kaamba koti anthu amamwa ndi kugwiritsa ntchito madzi osatetezedwa. Nkhani yowonjezera mosungira madziyo ndi yabwino chifukwa zikutanthauza kuti mtsogolo muno madzi sazidzavutavuta koma nkhawa ili pakuti anthu azigwiritsa ntchito chiyani? Nthawi zambiri madzi akasowa kumakhala mavuto aakulu, adatero Nkhata. Unduna wa zaumoyo wati nkhaniyi isachititse anthu kutayirira ndipo wati chofunika nkusunga madzi okwanira mmakomo mwawo kapena kugwiritsa ntchito njira zotetezera madzi. Pafupifupi mdera liilonse muli alangizi a zaumoyo choncho tiyeni tonse tiziwafunsa momwe tingatetezere madzi kuti tipewe matenda ammimba panyengoyi, adatero mneneri wa unduna wa zaumoyo, Adrian Chikumbe. Nthawi zambiri madzi akasowa, anthu amadalira zitsime kapena mitsinje yomwe madzi ake amakhala ndi dothi komanso tizilombo toyambitsa matenda ammimba. ",6 "Boma Lati Liyamba Kusunga Chiwerengero cha Anthu Ovutikisitsa Boma lati ndi koyenera kukhala ndi nambala ya anthu onse omwe ndi ovutikitsitsa mdziko muno. Makungwa: Pano tikupereka Mtukula Pakhomo Nduna ya za chiwerengero, mapulani ndi chisamaliro cha anthu mayi Mary Clara Mkungwa anena izi lachisanu ku Zomba pomwe amayendera ofesi yowona za kalembera ya National Statistical mu mzinda wa Zomba. Iwo ati kudziwa nambala ya anthuwa kuzithandiza kuti boma lidzitha kuwafikira anthuwa moyenera ndi thandizo losiyanasiyana lokhudza miyoyo yawo. Unduna umenewu ukugwira ntchito zake bwino kwambiri chifukwa sitipeka. Mwachitsanzo panopa timapereka Mtukula Pakhomo pomwe padakali pano timapereka kwa mabanja 28, 800 ndipo tufuna tizidziwa ngati tikufikiradi anthu ovutikisitsa mMalawi muno, anatero mayi Makungwa. ",14 "Chipatala Cha Pirimiti Chasankhidwa Kuti Chizisunga Odwala Nthenda ya COVID-19 Chipatala cha Pirimiti chomwe ndi cha mpingo wa katolika mu dayosizi ya Zomba chasankhidwa ndi boma kuti chikhale ndi malo osungira anthu omwe angapezeke ndi kachirombo ka Coronavirus. Mkulu wa chipatalachi Sister Mary Njukuna atsimikiza za nkhaniyi poyankhula ndi Radio Maria Malawi. Iwo ati padakali pano ntchito yokonza malowa ilimkati ndipo ayamba kugwira ntchito posachedwapa, pamene boma komanso bungwe la Save the Children alonjedza kuti athandiza ndi zipangizo zogwiritsira ntchito monga mabedi, ma face mask, ma glovesi ndi zina zambiri. Pirimiti inasankhiswa ndi boma kuti ikhale Isolation Center koma padakali pano siinayambe kutero popeza zipangizo sizinafike, anatero Sister Njukuna. Iwo ati akuyemnekezera kulandira chithandizochi kuchokera ku boma komanso kwa mabungwe omwe si aboma. ",6 " Anatchezera Sakuthandiza Agogo, Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndine mtsikana wa zaka 21 ndipo ndili ndi mwana mmodzi. Amuna anga adandisiya ataona kuti ndili ndi pathupi ndipo mwana atabadwa adauzidwa koma mpaka pano sadabwereko kudzaona mwana wawo. Ndikawauza za chithandizo samayankha, amangozengereza. Chomvetsa chisoni nchakuti munthune ndimakhala ndi agogo okalamba poti makolo anga onse admwalira. Ndithandizeni, ndipange bwanji? JS Mulanje Pepa JS, Apa zikuonekeratu kuti ngakhale ukuti amuna anga anthunu simunali pabanja ngakhale mumagonana mpakana kuberekerana mwana. Chimene chimachitika nthawi zambiri nchakuti atsikana akangogwa mchikondi ndipo mwamuna akangowauza kuti awakwatira, basi amaganiza kuti mwamuna ndi yemweyo basi ndipo amayamba zogonana naye ati pofuna kulimbikitsa chikondi kuti asamakaike za chikondi chawo, kumene kuli kulakwa kwakukulu. Atsikana ambiri aononga tsogolo lawo chifukwa cha mchitidwe wotere chifukwa anyamata kapena amuna ambiri ndi akamberembere, ongofuna kudzisangalatsa osalabadira za tsogolo la mnzawo. Akangomva kuti mtsikhana watenga pathupi basi, chibwenzi chimathera pomwepo. Zikatero mtsikana zako zada. Koma dziko lino lili ndi malamulo okhudza maukwati ndipo ngati wina wakuchimwitsa, ali ndi udindo woti akusamale komanso mwana. Ndiye apa usazengereze-pita ukadule chisamani kukhoti basi kuti chilungamo chioneke. Mwina amuna ena amene amakonda kuchimwitsa ana a eni akhoza kutengerapo phunziro! Akundikakamira Agogo, Ndine mtsikana wa zaka 19 zakubadwa, vuto langa ndi lakuti pali mnyamata wina wake amene amandifuna koma ineyo sindimamufuna olo pangono. Iye samafuna kuti angondisiya moti pano miyezi itatu yakwana akundifunabe. Nthawi zina ndimayesetsa kuti ndimuonetse nkhope yosangalala koma mtima wanga umakana. Ndiye nditani poti ine ndili naye kale amene ndimamukonda ndi mtima wanga wonse? Chonde ndithandizeni. MT Zomba Zikomo MT, Ndithudi akadakhalapo atsikana ambiri amaganizo ngati akowa bwenzi zinthu zikoma. Atsikana ambiri masiku ano amakonda kukhala ndi zibwenzi zambirimbiri ati kuti pamapeto adzasankhepo mmodzi. Chimenecho si chikondi ndipo mapeto ake ambiri amasokonezeka, mwinanso kutenga pathupi pa mnyamata amene samamukonda. Apa iwe waonetsa kale kuti ndiwe wokhwima mmaganizo ndipo ndikufuna kuti ndikulimbikitse kuti chikondi sakakamiza. Ngati uli kale ndi mnyamata amene umamukonda ndi mtima wako wonse palinso chifukwa chanji choti uzitaya nthawi ndi wina amene ulibe naye chidwi? Komabe nthawi zina chimachitika nchoti amene umamukonda kwambiri iye alibe chikondi, angofuna kukuseweretsa ndi kukometsa mawu a pakamwa ndipo amene sukumukonda ndi amene ali ndi chikondi chozama pa iwe. Ndiye apa chimene ungachite uyambe waona kuti bwenzi lakolo ndi munthu wotani? Ndi wamakhalaidwe otani? Ndi waulemu kapena ayi; ndi yo kapena wodzilemekeza; cholinga chanu ndi chiyani pa ubwenzi wanu? Chimodzimodzi amene ukuti akukukakamira chibwenziyo, kodi ndi munthu wotani? Cholinga chake ndi chiyani? Ndi wakhalidwe kapena mvundulamadzi chabe? Ukalingalira zonsezo bwinobwino mpamene ungasankhe chochita, chifukwatu nthawi zina umatha kukakamira mtunda wopanda madzi nkusiya munthu wachikondi weniweni. ",12 " Pepa Gaba, Malata Chalaka bakha nkhuku siyingatole. Nkhani ya Gabadinho Mhango ndi Lucky Malata ndiyo yatinenetsa mwambiwu. Msabatayi nkhani idawawasa ndi ya anyamatawa omwenso amasewera Flames. Akamunawa akadatola chikwama pangonongono ku Joni koma ena alepheretsa. Aganyu sitinadandaule koma pena sitikumvetsa njomba yomwe yaseweredwa apa. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Ife sitidamvepo wosewera chigawo cha pakati atalowera kummwera kukayesa mwayi ndi Blantyre United koma pakutha pa mwezi kumva kuti wayesera mwayi ndi Big Bullets, Mighty Wanderers, Azam Tigers mpaka kufunanso kukadoda ku Evirom. Lero Gaba wapita ku Joni koma museweretseni matimu ambirimbiri. Kodi zidatero chifukwa chiyani? Kodi timu zonsezi zimamufuna pakamodzi? Kodi zimachitika mwa chiponyeponye kuti kugwere mwayi ndi komweko? Tikumva kuti matimu ena amafuna wosewera ngati Didier Drogba osati luso la Gaba. Koma izi ndi zoona? Ngati amafuna woteroyo bwanji osangopita ku Ivory Coast kukatenga Drogba? Kodi ndizotheka Gaba kusewera ngati Drogba? Gaba ndi Gaba ndipo Drogba ndi Drogba, sangafanane. Tikuganiza kuti chilipo chomwe chimachitika kuti Gaba ndi Malata azingowavinitsa. Ku Amazulu pa magemu 5 Gaba adachinya zigoli 4 ndiye apapa akufunanso chiyani? Komanso tikudabwa kuti bwanji Fam imangowonerera izi zikuchitika? Komadi Fam ndi manthu wa zamasewero mdziko muno? Kodi zidachitikapo zoterezi? Tithokoze kuti mwabwerako muli moyo. Pepani kuti mwavina moteromo koma dziwani kuti chitseko chitha kutseguka. Dekhani timu zokoma zipezeka. Osadanda posakhalitsa tidzikuwonerani pa SuperSport mukumakana ndi Messi kapena Ronaldo. ",16 "Khonsolo ya Zomba Isankha Anthu Olondoloza Chitukuko Wolemba: Thokozani Chapola Khonsolo ya boma la Zomba yayamba ntchito yosankha anthu oyanganira zitukuko mmadera a mafumu aakulu onse mbomalo. Polankhula pa chisankhochi mfumu yaikulu Mlumbe yalangiza adindo atsopanowa kuti apewe kukondera pa ntchito yawo. Iwo apemphanso aphungu a kunyumba ya malamulo komanso makhansala kuti azigwiritsa bwino ntchito ndalama za chitukuko zomwe amalandira ponena kuti pali zitukuko zina zomwe zimalephereka kaamba koti adindowa asokoneza ndalamazi. A ndale amayima pa chulu kulengeza kuti achita chakuti pomwe ndi zabodza. Zomwe akaupanga a ndalewa akutipha ife anthu a kumudzi zomwe zikuchititsa kuti dera langa la Zomba Changalume lisatukuke. Ananenapo kuti atsegulira police unit, bridge komanso sukulu ya sekondale zonsezo zili za bodza zenizeni palibe chomwe chamngidwa olo ndi chimodzi chomwe, inadandaula motero mfumu yaikulu Mlumbe. Polankhulapo yemwe wasankhidwa kumene pa udindowu mdera la mfumu yaikulu mwambo a Frederick Naoje alonjeza kuti agwira ntchito yawo posayangana mtundu kapena chipani. Ntchito yanga ndi yolondoloza chitukuko ndip ndiwonetsetsa kuti pasakhale tsankho koma aliyense apindule pa chitukuko chilichonse chomwe chingabwere ku dera kuno, anatero a Naoje. Chisankhochi chachitika ndi thandizo lochoka ku Local Government and Accountability Performance (LGAP). ",2 " Bullets yayamba ndi ukali Timu ya Big Bullets, yomwe ikuteteza chikho cha TNM Super League, yayambanso ndi ukali mndime yachiwiri ya ligiyi, kupitiriza zomwe idachita mndime yoyamba. Timuyi idachapa Mafco ku Dwangwa komwe ndime yachiwiri ya ligiyi idakakhazikitsidwa. Bullets idapambana 1-0 ndipo pano yaonjezera mapointi kufika pa 35. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Bullets ili ndi mapointi 7 pamwamba pa Azam Tigers, yomwe ili ndi mapointi 28. Koma Azam yamenya magemu ochuluka ndi imodzi kuyerekeza Bullets. Azam idalepherana mphamvu ndi Kamuzu Barracks komanso Epac FC kuti ibwerere ku Blantyre ndi mapointi awiri kuchokera ku Lilongwe. Mmodzi wa makochi a timu ya Bullets, Mabvuto Lungu, adati chomwe akufuna kuchita nkuteteza mbiri yawo yosagonja. Bullets sidagonjepo mndime yoyamba ya ligiyi. Matimu onse akonzekera zofuna kugonjetsa Bullets, ndipo akubwera mokonzeka kuti akwaniritse zomwe akufuna. Komabe tiyesetsa kuti mbiri yathu isasinthe, adatero Lungu pouza Tamvani. Mawa timuyi iswana ndi Red Lions pa Kamuzu Stadium. Mndime yoyamba Bullets idalepherana mphamvu ndi timuyi 1-1 ku Zomba. Timu yomwe Bullets imalimbirana nayo ufumu mumzinda wa Blantyre, Mighty Be Forward Wanderers, yayamba moipa mmdimeyi pamene idagonja ndi Civo United 1-0 pa Kamuzu Stadium sabata yatha. Lero Wanderers, yomwe ili ndi mapointi 26, ndipo ili pa nambala 5, pamndandanda wa momwe matimu akuchitira mligiyi, ichapana ndi Kamuzu Barracks, yomwe ili ndi mapointi 23. Masewerowo ali pa Kamuzu Stadium. Matimu ena amene ayamba molakwika ndi Dedza Young Soccer, yomwe idagonja ndi Red Lions. Mawa Young Soccer ndi Silver Strikers pa Silver Stadium. Anyamata a ku Dedzawa ali panambala 11 ndi mapointi 15. FISD Wizards nayo yayamba ndi kulira pamene idaswedwa ndi Civo 1-0 pa Kamuzu Stadium. Lero FISD itengetsana ndi Moyale ku Mzuzu ndipo mawa ikutikitana ndi Mzuni FC pabwalo lomwelo. FISD ili kunsonga kwa ligiyi ndi mapointi 9 okha. Mzuni ili panambala 15 ndi mapointi 11 pamene Moyale ili pa nambala 10 ndi mapointi 19. Mzuni ndi Moyale onse adaswedwa ndi Silver sabata yathayi. Nayo Airborne Rangers idathotholedwa nthenga nkugwa itatibulidwa ndi Blue Eagles 3-0. Lero Airborne ikulandira Epac ku Dwangwa pa Chitowe. Timuyi ili ndi mapointi 13 ndipo ili panambala 12, pamene Epac ili panambala 13 ndi mapointi 12. Lero maso akhale pa Kamuzu Stadium ngati Bullets ipitirire kuchita bwino pamene ikuswana ndi mikango ya ku Zomba, Red Lions. ",16 " Zipani zikufuna machawi pa chisankho Zipani zandale zati bungwe loyendetsa zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) lichititse msanga chisankho chobwereza kudera la kummwera cha ku mmawa kwa Lilongwe kuti anthu akuderari akhale ndi phungu owayimirira ku Nyumba ya Malamulo. Izi zikutsatira chigamulo cha bwalo lalikulu la apilo kuti chisankho cha phungu wa deralo chichitikenso litaunika dandaulo la yemwe ankayimirira chipani cha Malawi Congress Party (MCP) Ulemu Msungama kuti chisankhocho sichidayende bwino. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Sipikala wa Nyumba ya Malamulo Richard Msowoya watsimikiza kuti kutsatira chigamulochi, deralo tsopano lilibe phungu. Bwalo lomwe lagamula ndi lalikulu mdziko muno kutanthauza kuti kulibenso komwe nkhaniyo ingalowere. Apa, zikutanthauza kuti kuderako kulibe phungu nchifukwa chake kuchitikenso chisankho, adatero Msowoya. Pachisankho cha pa 20 May, 204, bungwe la Mec lidalengeza kuti Bentley Namasasu yemwe ankayimira chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) ndiye adapambana koma Msungama adakamangala kubwalo la milandu za chigamulochi. Wachiwiri kwa mlembi wa chipani cha MCP Eisenhower Mkaka adati bungwe la MEC lisakoke nkhaniyo koma kuthamangitsa chisankhochi kuti anthu a mderalo akhale ndi phungu owayimilira ku Nyumba ya Malamulo. Mneneri wa chipani cha Peoples Party (PP) Noah Chimpeni adati MEC iyambirepotu kusakasaka ndalama zopangitsira chisankhochi mawu omwe adagwirizana ndi a mneneri wa chipani cha UDF Ken Ndanga. Apa MEC iyambiretu kusakasaka ndalama zopangitsira chisankhochi munthawi yake kuti ikwaniritse ntchito yake malingana ndi malamulo, adatero Ndanga. Chikalata chomwe MEC idatulutsa Lachitatu, chidati pali z ofunika kutsata chisankhochi chisadachitike. Aka kakhala koyamba kuti chisankho cha mtundu uwu chichitike mumbiri ya Malawi. Motero, tikuyenera kuunika bwino chigamulochi ndi malamulo oyendetsera chisankho kuti akutinji, chidatero chikalatacho. Mneneri wa bungwelo Sangwani Mwafulirwa adati malamulo sanena nthawi yeniyeni yofunika kutenga kuti chisankho chotere chichitike ndipo mmalo mwake akhoza kugwiritsa ntchito lamulo lomwe limati pasadathe masiku 60. Mwafulirwa adatinso mwa zina, bungweri likufunika kuti lisake ndalama zopangitsira chisankhochi chifukwa mundondomeko ya chuma ya 2016 mpaka 2017 mulibe pologalamu yachisankhochi. ",11 " Ambwandira msilikali ku Salima Apolisi a chigawo chapakati abatha msilikali wa nkhondo ndi anthu ena awiri powaganizira kuti adapezeka ndi chamba popanda chilolezo. Msilikaliyu, Alex Kanjanga wa zaka 23 wagwidwa ndi majumbo 16 a chamba pachipikisheni cha polisi pa Thavite mboma la Salima. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mneneri wa polisi mchigawo chapakati Noriet ChihanaChimala watsimikiza za nkhaniyi ndipo wati tsiku lomwe msilikaliyu adagwidwa pa 3 April 2018, apolisiwo adagwiranso Lawrent Medson Tambala wa zaka 30 atamupeza ndi majumbo 11 achamba komanso Mary Mwambane wa zaka 28 atamupeza ndi katundu yemwe akuganiziridwa kuti adabedwa. Chimala wati apolisi adakhazikitsa malo achipikisheni adzidzidzi pa Thavite ndipo katundu yenseyo adapezeka pachipikishenicho ndipo anthu onsewa akawonekera ku khoti kafukufuku akatha. Kanjanga yemwe akugwira ntchito ku Engineers Battalion yomwe ili mboma la Kasungu amachokera mmudzi mwa Msongola kwa mfumu Kwataine mboma la Ntcheu. Tidamupezanso ndi njere za chamba, adatero Chimala. Iye adati pamalopo, adagwiranso Tambala akuchokera ku Nkhotakota ndipo iye adabisa majumbo achambawo mchikwama chomwe amayenda nacho paulendowo. Malingana ndi Chimala, Tambala amachokera mmudzi mwa Kapangalika, kwa mfumu Khongoni mboma la Lilongwe ndipo naye akuyembekezera kafukufuku wapolisi kuti akawonekere ku khoti. Awiriwa awatsegulira mlandu wopezeka ndi chamba popanda chilolezo chilichonse. Pachipikisheni china patsikulo, apolisi adapeza zipangizo zowotchererera mchikwama cha Mwambane koma iye adalephera kufotokoza komwe adatenga zipangizozo ndipo apolisiwo adamutengera ku polisi ya Salima. Ndi ntchito yapolisi kulondoloza komwe katundu wachokera, ngati munthu akulephera kuonetsa malisiti ogulira kapena kufotokoza bwino komwe watenga katundu yemwe alinaye, amayenera kutengedwa kuti akalongosole bwino za katunduyo, watero Chimala. Mwambane amachokera mmudzi mwa Mbuna, kwa mfumu Kanyenda mboma la Nkhotakota ndipo akuyembekezeka kudzayankha mlandu wopezeka ndi katundu oganiziridwa kuti adabedwa kafukufuku wapolisi akatha. ",15 "Papa Apempha Madotolo Kuti Akhale Okhulupirika Wolemba: Sylvester Kasitomu Papa Francisko lachisanu lapitali wapempha madotolo kuti apewe mchitidwe wothandizira odwala kuti amwalire mwamsanga powapatsa mankhwala olakwika, ponena kuti kutero ndikuonetsa khalidwe loipa. Papayu wayankhula izi pa nkumano wake ndi ma madotolo omwe anakamuchezera kulikulu la Mpingowu ku Vatican. Iye wati mchitidwe wothandizira odwala kuti amwalire mwamsanga maka kubaya kapena kupereka mankhwala olakwika ndi wonyazitsa ulemerero wa munthu womwe ndi tempile ya mulungu. Mtsogoleri wa mpingo wakatolikayu mwazina watsindika za kufunika kolemekeza moyo wa munthu wina aliyense maka pozindikira kuti Mulungu ndiye mwini moyo ndipo kuti palibe munthu yemwe ali ndi mphamvu yothandizira kuti munthu amene akudwala amwalire mwa msanga chifukwa chakukula kwa matenda komanso palibe yemwe ali ndi mphamvu yochotsa moyo wa munthu. Iye wati ndi Mulungu yekha yemwe amapereka moyo ndipo ndi yemweyo amatenganso moyo pa nthawi yake. Papayu wapitiriza kunena kuti kusamalira wodwala sikungopereka mankhwala kokha komanso kumvetsera ndi chidwi nkhawa za wodwala aliyense payekhapayekha. Iye wakumbutsa madotolowo kuti nthawi zonse ayenera kukumbukira malamulo a ntchito yawoya udotolo. Pamwambowo panali madotolo ochiza matenda osiyanasiyana okwana 350 a mdziko la Italy. ",6 "Magufuli Wati Chiwerengero Cha Atsikana Otenga Mimba Chakwera Kwambiri Ku Tanzania Wolemba: Sylvester Kasitomu 9768"" src=""http://www.radiomaria.mw/wp-content/uploads/2019/10/magufuli.jpg"" alt="""" width=""537"" height=""358"" />Wauza apolisi amange aliyense opeereka mimba kwa atsikana apasukulu-Magufuli President wa dziko la Tanzania a John Pombe Magufuli wati ndi wokhudzidwa kaamba kakukula kwa chiwerengero cha atsikana omwe akutenga pathupi ali pa sukulu chomwe akuti chafika pa 2 hundred 29 mu chigawo chimodzi chokha cha dzikolo. President Magufuli wati ndi zomvetsa chisoni kwambiri kuti azibambo ena sakuona kufunika kolimbikitsa maphunziro a tsikana mdzikolo ndipo mmalo mwake akukhala patsogolo powononga tsogolo lawo. Malinga ndi BBC, Magufuli wadzudzula azibambo omwe akupezeka ku chigawo cha kuzambwe kwa dzikolo kuti ndi omwe akukhala patsogolo kwambiri kumagonana ndi ansungwana omwe ali msukulu zosiyanasiayana mdzikolo. Pamenepa President Magufuli walamula asilikali adzikolo kuti amange azibambo onse omwe apezeke olakwa popereka mimba kwa atsikana apasakulu. Dziko la Tanzania limapereka maphunziro aulere kwa atsikana opezeka msukulu zosiyanasiayana mdzikolo. ",14 "Bonongwe Wadzudzula Boma Kamba Kosaika Chidwi pa Ulimi Mmodzi mwa anthu omwe amalankhulapo pa nkhani zokhudza ulimi mdziko muno Mathius Bonongwe wadzudzula boma kaamba kosayika chidwi chokwanira pa nkhani za ulimi mdziko muno. Bonongwe walankhula izi pothilirapo ndemanga pa ndondomeko ya za chuma ya 2020/2021 yomwe nduna ya za chuma a Joseph Mwanamvekha anapereka ku nyumba ya malamulo lachisanu pa 12 June 2020. Akuti boma silinaganizire alimi ngati awa Mu ndondomekoyo boma layika 194.9 Billion kwacha ku gawo la za ulimi ndipo mwa ndalamazi, 48.8 Billion kwacha ndi zogulira chimanga, kuyendetsera ndondomeko ya zipangizo za ulimi zotsika mtengo ya FISP komanso kulimbana ndi tizilombo towononga mbewu. Pamenepa Bonongwe wati ndalama zomwe boma layika ku gawo la za ulimi ndi zochepa poyerekeza ndi mavuto omwe alimi mdziko muno akukumana nawo. Boma limayenera liyangane kwambiri mavuto amene ali mmidzi kamba koti mMalawi muno anthu ambiri ndi osauka koma atenga anthu ochepa chabe kuti apindule mu ndondomeko imeneyi ya feteleza sabuside, anatero a Bonongwe. Iwo apemphanso unduna wa zaulimi kuti uyike ndondomeko zokhwima ndi cholinga choti mchitidwe ogula ma kuponi kwa alimi uchepe kamba koti anthu omwe amagawa ma kuponi ndi omwewonso amapita kumakawagula alimi ovutika makuponi mmidzimo zomwe akuti ndi zochititsa kutu umphawi usathe mdziko muno. ",4 " A ku Mozambique akulembetsa mavoti Mwafulirwa: Ndi mlandu waukulu Nzika zina za mdziko la Mozambique zikulembetsa nawo mkaundula wa mavoti ku Dedza popofuna kuti zidzavote nawo pa chisankho cha magawo atatu chomwe chilipo pa 20 May, 2014. Mneneri wa polisi ku Dedza Edward Kabango wati panopa apolisi anjatapo kale nzika imodzi ya dzikokolo, Edward Tenganibwino, wa zaka 28, wochokera mmudzi mwa Golongozo yemwe amafuna kulembetsa mkaundulayu mwachinyengo. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Kabango wati Tenganibwino adanamiza akalaliki ochita kalemberayu kuti ndi Mmalawi ndipo amachokera mmudzi mwa Katsekaminga ku Dedzako koma akalalikiwo adamuzindikira msanga ndi kumuneneza kupolisi. Bungwe logwira ntchito zophunzitsa anthu la National Initiative for Civic Education (Nice) lati nzika zambiri za ku Mozambique zalowa mdziko muno kufuna kudzalembetsa nawo koma zina zidabwezedwa akalaliki a kalemberayu atazitulukira. Mkulu woyendetsa za maphunziro kubungweli, Patrick Siwinda, wauza Tamvani kuti asanu agwidwapo kale koma ena akadali zungulizunguli mbomalo kuyesayesa kuti alembetse mkaundulayu. Iye wati ambiri mwa anthuwa akuti amafuna ziphaso zoponyera voti ndi cholinga choti azidzatha kutenga ngongole zotukulira ulimi wa kachewere kumabanki a mdziko muno. Siwinda wati ambiri mwa anthu achinyengowa akumagwiritsa ntchito ziphaso zolowera ndi kutuluka mdziko za Malawi komanso ziphaso zoponyera voti za mndondomeko ya chisankho cha chaka cha 2009 ngati umboni kuti awalembe. Pa 2 November, bambo wina wa ku Mozambique adabwera ndi chiphaso cha ku Malawi kuti alembetse koma adabwezedwa, adatero Siwinda. Iye adati nthumwi za bungweli zati mchitidwewu ukuoneka mmalo olembetserako 13 a mdera la Bembeke. Siwinda wati madera omwe akukhudzidwa ndi mchitidwewu ndi Katsekaminga CDSS, Mazanjala, sukulu zapulayimale za Kapesi ndi Magaleta, sukulu zasekondale za Umbwi, Msambiro, Dedza Muslim Jamat, sukulu ya asungwana Achisilamu ya Dedza, Dedza CCAP, Dedza LEA, Dedza Community Hall ndi mudzi wa Dauya. Bungwe loyendetsa zisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) lati mchitidwe wolembetsa kapena kuthandizira munthu yemwe sali woyenera kulembetsa kuti alembetse ndi mlandu waukulu ndipo wolakwa akhoza kunjatidwa. Wofalitsa nkhani mbungweli Sangwani Mwafulira wati pofuna kuchepetsa mchitidwewu, zipani ndi mabungwe azisankha oyanganira ndondomeko ya chisankho (monitors) kuchokera mdera lomwe kukuchitikira ntchitoyi kuti azitha kuzindikira anthu ofuna kuchita zachinyengo. Ndi bwino kusankha nthumwi za mdera lomwe kukugwiridwira ntchitoyi chifukwa sizivuta kuzindikira anthu. Komanso anthu akuyenera kuzindikira kuti kuperekera umboni wabodza kuti munthu ndi Mmalawi pomwe si Mmalawi woyenera kulembetsa mkaundula ndi mlandu waukulu woti munthu akhoza kulipira ndalama zokwana K500, 000 kapena kukakhala kundende zaka ziwiri, watero Mwafulirwa. ",11 " Mdima wanyanya mmakhonsolo Zomwe anena a makhonsolo a mizinda ya Lilongwe Blantyre ndi Mzuzu zikusonyeza kuti vuto la mdima mmisewu ya mizindayi litenga nthawi kuti lithe kaamba koti, ngakhale akuyesetsa kuti akonze zinthu, anthu ena akubwezeretsa zinthu mmbuyo poononga dala zipangizo za magetsi. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Escom in free-for-all fuel scam Khonsolo ya mzinda wa Lilongwe yati vuto lalikulu ndi nthawi yomwe kampani ya magetsi ya Escom imatenga kuti ikalumikize magetsi ntchito yozika mapolo ikatha. Mneneri wa khonsoloyi, Tamala Chafunya, wati khonsolo ikamaliza kuzika mapolo nkulumikiza nthambo za magetsi, zimakhala mmanja mwa Escom kuti idzamalizitse ntchitoyo polumikiza magetsiwo. Gawo lathu pa ntchito imeneyo idachitika ndipo kuchedwaku ndi kampani ya Escom. Khonsolo idalipira kale ndalama zolumikizira magetsi koma zaka zikungopita ngakhale kuti timayesetsa kutokosako, adatero Chafunya pouza Tamvani pa nkhani ya vuto la mdima mmisewu yambiri mumzindawu. Chafunya adati kuchedwaku kumapereka danga kwa anthu amaganizo olakwika kuti aziononga mapolowo ndipo chipsinjo chimagweranso pamsana pa khonsolo kukonzanso mapolowo. Mneneri wa kampani ya Escom Kitty Chingota adavomereza kuti khonsoloyi idalipiradi ndalama zolumikizira magetsi koma akatswiri ake atakayendera malo ofunika kulumikiza magetsiwo adapeza zolakwika zambiri. Iye adati pofuna kupewa ngozi za magetsi, kampaniyi idalangiza khonsoloyi kuti ikonze molakwikamo magetsewo asadabwere koma palibe chomwe achitapo. Mmalo ena mapolo adadutsa mmunsi mwenimweni mwa nthambo zathu za magetsi ndipo malamulo a Escom salola kulumikiza magetsi mmalo oterewa. Mmalo ena mapolo adatalikirana kwambiri chifukwa ena adagwetsedwa ndi anthu opotoka maganizo ndiye mpovuta kulumikiza magetsi mmalo oterewa, adatero Chingota. Koma Chafunya adati nthawi zambiri mapolowo akawonongedwa kumakhala kovuta kuwabwezeretsa chifukwa ndalama zomwe zimalowa nzochuluka kwambiri. Kukonza polo ya simenti imodzi yokha, kuyambira kuwumba mpaka kukaizika, imatenga ndalama zokwana K400 000 ndiye muwerengere kuti msewu umodzi umadya ndalama zingati za mapolo, nanga anthu akawononga kuti tikabwezeretse ndiye kuti zitukuko zina ziimiratutu, adatero Chafunya. Mumzinda wa Blantyre nkhani ndi yokhayokhayi; mmisewu yambiri ndi mdima wokhawokha kaamba koti mapolo ambiri adagwtsedwa ndi akuba, zomwe zikuchititsa kuti ena azichitidwa chipongwe chifukwa cha kusowa kwa kuwala usiku. Mneneri wa khonsoloyi Anthony Kasunda adati nzoona kuti mumzindawu muli vuto la magetsi mmbali mwa misewu chifukwa ambanda adaba zipangizo pamapolo. Ili ndi vuto lalikulu chifukwa anthu amayenda mwamantha usiku. Pamene khonsolo ikuyesetsa kuti ngati mzinda tipite patsogolo ndi chitukuko, anthu ena amaganizo olakwika akubwezeretsa chitukuko mmbuyo pomaba zipangizo ngati zothandizira magetsi a pansewu, adatero Kasunda. Iye adati ngati khonsolo akupempha a makhoti kuti pamene munthu wagwidwa ndi katundu wa khonsolo, ameneyo azilandira chilango chokhwima kuti asadzabwerezenso, komanso kuti ena atengerepo phunziro. Komanso tikufuna tipeze njira imene tingachite kuti zipangizo za magetsi zisamabedwe monga pogwiritsa ntchito magetsi oyendera mphamva ya dzuwa ija pa Chingerezi amati solar powered system. Pempho lathu ngati khonsolo ndilakuti tiyeni tonse titengepo gawo poteteza katundu kapena zipangizo zimene khonsolo imaika mmalo osiyanasiyana kuti zitumikire anthu okhala mumzinda wa Blantyre. Isakhale ntchito ya khonsolo yokha koma tonse, adatero Kasunda. Namonso mumzinda wa Mzuzu nyimbo ndi yokhayokhayoambanda ali kaliriki kuononga zida za magetsi mmbali mwa misewu moti malo ambiri mdima uli bii usiku ukagwa. Zinthu zidayamba kusonya pamene magetsi oyamba mmisewu ya mmataunishipi monga Zolozolo, Chimaliro, Katawa ndi Msongwe adayatsidwa mu 2012 ndi 2013, koma pano zinthu zabwerera mmbuyo chifukwa anthu ena adayamba kuba nthambo za magetsiwa. Wogwirizira mpando wa mkulu wa khonsoloyi, Victor Masina, adati ili ndi vuto lalikulu ndithu moti pano a khonsoloyi akufuna ndalama zosachepera K3.5 miliyoni kuti akonzenso zipangizo zoonongekazo monga ma transformer ndi mapolo ogwetsedwa ndi galimoto zikaphuluza msewu. ",2 "HRDC Yapempha Boma Kuti Liyimitse Chiganizo cha Lockdown Bungwe lomenyera ufulu wa anthu mdziko muno la Human Rights Defenders Coalition (HRDC) lati boma liyimitse kaye ganizo lake loletsa anthu kuyendayenda ndi kuchita ntchito zawo kapena kuti Lockdown pachingerezi kuti lipereke kaye tsatanetsatane wa mmene lithandizire anthu mu nthawiyi. Wachenjeza boma-Trapence Boma, lidalengeza kuti kuyambira pakati pa usiku wa loweruka pa 18 mwezi uno mpaka pakati pa usiku wa pa 9 May chaka chino anthu asayendeyende,omwe ndi masiku 21,pofuna kuchepetsa kufala kwa nthenda ya COVID-19. Polankhula pa msonkhano wa atolankhani lero mmawa, wapampando wa bungweli Gift Trapence,wati bungweli lawuza kale maloya ake kuti apite ku bwalo la milandu kuti lilowelerepo pa nkhaniyi ponena kuti boma ladya mfulumira polengeza za ganizoli lisadaike mfundo zothandizira anthu osauka pa nthawi yosayendayendayi. ",11 "ECM Yati Mapemphero a Sabata Yoyera Achitika Likulu la mpingo wakatolika mdziko muno la Episcopal Conference of Malawi (ECM) lati miyambo yonse ya mapemphero mu Sabata Yoyera mu nyengo ya Lent ichitika potsatira dongosolo loti pa miyamboyi pasamakhale anthu oposera zana limodzi (100). Alemba chikalatacho-Bambo Saindi A kulikulu la mpingowu ku Episcopal Comference Of Malawi ECM ndi omwe anena izi kudzera mu chikalata chomwe atulutsa ndipo chasainidwa ndi mlembi wamkulu wa bungwe la maepiskopi a mpingowu mdziko muno, bambo Henry Saindi. ",13 " Chipwirikiti ku Malawi Kuphwanya ndi kusalemekeza malamulo kwayala nthenje mdziko muno. Anthu akungopha ngati akupha nkhuku, kugwiririra, kuononga ngakhalenso kuyatsa katundu. Sabata yatha, anthu awiri adakhapidwa ndi kuphedwa ku Neno powaganizira kuti ndi mfiti ndipo sipanathe nthawi pomwe anthu enanso adaphedwa kwa Chitukula ku Lilongwe pamkangano wa malo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Naye adagendewa: Mayaya Izi zili apo, Akhristu ndi Asilamu adalikitana ku Balaka pomwe sukulu ya mpingo wa Anglican ya Mmanga idaletsa atsikana kuvala mipango yotchinga kumutu potsatira chipembedzo cha Chisilamu. Ndipo izi zili mkamwamkamwa, msilikali wina adapha asilikali anzake awiri ku Ntcheu ndipo naye adaomberedwanso ndi apolisi a kuusilikali. Ndipo si kale pomwe nyumba 21 zidaotchedwa ku Nkhata Bay ndipo anthu 4 adaphedwa pa zipolowe. Si kale pomwe anthu otsatira chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) adagenda ndi kuvulaza mmodzi mwa omenyera ufulu wa anthu Billy Mayaya pa zionetsero zimene bungwe la Human Rights Defenders Coalition (HRDC) limachita pofuna kukakamiza mkulu wa bungwe la Malawi E;ectoral Commission (MEC) Jane Ansah atule pansi udindo. Ndipo wapolisi wina adaphedwa ku Nsundwe mboma la Lilongwe pomwenso apolisi ena akuwaganizira kuti adagwirira ndi kulanga amayi ndi asungwana ena. Nako ku Karonga, pofuna kusatsalira pa mpungwepungwe wabukawu, kudali anthu ena kuvula amayi ndi atsikana ngati avala mathalauza ndi siketi zazifupi mbomalo. Izi zikuchitika ngakhale lamulo loyendetsera dziko lino limati kuli ufulu wa kavalidwe. Ndipo amabungwe oteteza ufulu wa anthu monga Foundation for Community Support Services (Focus) adzudzula mchitidwewu ndipo apempha apolisi kuti atsekere mchitokosi wachinyamata aliyense amene akuvula amayi. Pakadalipano mkulu wa apolisi mbomalo Sam Nkhwazi wati sadamangeko munthu pokhudzana ndi nkhaniyi. Malinga ndi Mfumu Malema 2 ya mboma la Karonga, iwo adakhazikitsa malamulo woti ana a sukulu (anyamata ndi atsikana) asamapezeke kunyanja chifukwa zinthu zidafika poipa ndipo anawa amachita zolaula kunyanjako. Iye adati atakhala pansi adakhazikitsa gulu lomakayendera kunyanjako ndi kumagwira tiana tomwe amatipeza komanso adapeza galimoto yomwe idalengezetsa Lachisanu lapitalo kuti anawa asapezeke kunyanja ndipo akangopezeka agwidwa. Tidachita izi chifukwa anawa adaonjeza kuthawa kusukulu nkumabwera kunyanja kukamwa mowa ndi kugona ndi amuna. Chidatikhudza kwambiri ndi choti mwana wina wa zaka 13 adamwetsedwa mowa patsiku la anakubala ndi kugonedwa ndi anyamata ambiri. Anawa amakhala oti athawa msukulu, adatero Malema. Koma iye adakanitsitsa kuti adakhazikitsa malamulo oti amayi asamavale mathalauza ndi siketi zazifupi mbomalo. Izo akupanga ndi akabaza kumsika ndipo ife sizikutikhudza, adatero iye. Pomwe mayi wina yemwe adaona mnzake akuvulidwa, Christobel Shaba, adati zikuchitika mbomalo ndi zoopsa ndipo amayi akukhala ndi mantha akulu. Polankhulapo pa chipwirikiti chomwe chikuchitikachi, mphunzitsi wa ufulu wa anthu pasukulu ya ukachenjede ya University of Livingstonia George Phiri adati zonsezi zikungosonyeza kuti utsogoleri wa dziko lino walephera. Phiri adatinso nzokhumudwitsa kuti mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika sakuonetsa chidwi chofuna kuthetsa mavuto mdziko muno ndipo wangoti duuu! Tangoganizani, wamkulu wa apolisi adabwera poyera nkunena kuti apolisi alibe kuthekera kopereka chitetezo mdziko muno, kodi mtsogoleri wa dziko lino adachitapo chiyani izi zitanenedwa? Kodi mtsogoleriyu akuona zikuchitikazi? Nanga bwanji wangoti duuu! ndipo palibe chomwe akuchitapo? adatero Phiri. Koma nduna ya zofalitsa nkhani Mark Botomani idatsutsa kwa mtu wa galu kuti utsogoleri wa dziko lino walephera. Botomani adati ngakhale akugwirizana ndi zoti zikuchitika mdziko muno ndipotsa mantha komanso zoziziritsa thupi chifukwa anthu akungotengera malamulo mmanja mwawo, koma mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika akuyesetsa kukonza zinthu kuti zibwelere mchimake. ",15 " Anatchezera Akundifunanso Anatchereza, Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Telemu yotsiriza ya Fomu 3 ndidapalana ubwenzi ndi mtsikana wina pasukulu yathu ku Mulanje. Koma tikuyandikira kulemba mayeso a Fomu 4, bwenzi langalo lidanditumizira uthenga palamya kundiuza kuti chibwenzi chatha chifukwa sindine mwamuna. Iye adaonjezera kuti pomwe ankandilola nkuti ali ndi chibwenzi china. Izitu zidandiwawa kwambiri chifukwa tinkalonjezana kuti tidzakwatirana. Chondivuta nchoti atangomva kuti ndayamba ntchito adayambanso kundiimbira foni nkumandiuzakuti chikondi chake pa ine sichidathe. Ndichite chiyani pamenepa? DF, Mulanje. DF, Nthawi zonse ndimalangiza amene ali msukulu kuti ayenera kupewa mchitidwe wokhala ndi zibwenzi. Izi ndimanena makamaka chifukwa zimasokoneza maphunziro. Taonani apa mukuti mtima wanu udasweka mutayandikira kulemba mayeso a Fomu 4 mkaziyo atathetsa chibwenzi. Sindikukaika konse kuti izi zidakhudza momwe mudakhonzera mayeso a Fomu 4. Simukadakhonza kuposa momwe mudachitira mutakhumudwa ndi kuthetsa kwa chibwenzi kumene mudakumana nako. Tsono funso lanu mukuti muchitenji? Langizo langa ndi loti, musataye nthawi ndi mtsikanayo chifukwa waonetseratu kuti ndi wamadyeramphoto komanso ali ndi mtima wa chimasomaso. Adakuuzani kuti adakulolani ngakhale adali ndi chibwenzi china panthawiyo. Tsono, muli ndi chitsimikizo chotani kuti mukadzakwatirana naye sakapezanso mwamuna wina wamseri? Taonani adati inu si mwamuna pomwe amathetsa chibwenzi. Tsopano akukusakani chifukwa mwapeza ntchito. Kodi mutakwatirana naye, ntchitoyo nkutha ameneyo sadzakuthawani? Samalani naye mkazi wa chimasomaso! Zikomo Gogo, Ndidapanga chibwenzi ndi mkazi wina yemwe ali ndi mwana mmodzi. Chithereni ukwati wake woyamba, patha chaka ndi miyezi ingapo. Mgwirizano wathu ndi woti tidzamange banja. Koma tsiku lina ndikuchokera kuntchito ndidangolowa mnyumba osagogoda ndipo ndidamupeza akulankhula pafoni. Adadzidzimuka nkudula foniyo koma nditamulanda ndidaona kuti amalankhula ndi mwamuna wake woyambayo. Ndidamuuziratu kuti chibwenzi chatha ndipo azipita kwawo. Adagwada nkulira kunena kuti ndimukhululukire sadzayambiranso. Iye adati mwamunayo amaimba kufuna kudziwa njira yopita kwa mayi anga kuti akaone mwana. Ndichitenji, mundiyankhe pafoni pomwepa. G, Lilongwe Zikomo a G, Poyamba, ndikukumbutseni kuti ndi zovuta kuti aliyense amene wandifunsa ndi zimuyankhanso pafoni. Izi zili choncho chifukwa ndimalandira mafunso ambiri choncho kuti aliyense ndizimuyankha pafoni sizingatheke. Palinso ena amafulasha, tsono ine kuti ndiziimbira aliyense amene akufulasha, ndiwo ndigula? Tsono kubwera ku funso lanu, poyamba ndikudabwa kuti mukukhala bwanji ndi mkazi amene simunalongosole zaukwati? Kodi mutapatsana mimba, sipakhala mavuto ena? Izi zili choncho, mudziwe kuti mkaziyo akunama kuti amapereka njira ya komwe mayi akukhala kwa mwamuna wake wakale. Tiziti nthawi yonse adali limodzi, mpaka mwana mwamunayo samadziwa pakhomo pa mayi a mkazi wake? Akadakhala kuti amakambirana za njira bwanji adadula foniyo? Samalani. Ofuna mabanja Ndikufuna mkazi koma akhale wa zaka 17. Pepani sindiika nambala yanu chifukwa mwati mukufuna mkazi wa zaka 17. Ameneyo si mkazi koma mtsikana ndipo malamulo a dziko lino akuletsa kuti ana osakwana zaka 18 asamakwatiwe. Ndine mwamuna wa zaka 28 ndipo ndili pantchito ku Lilongwe. Ndikufuna mkazi wopanga naye ubwenzi mpaka banja. ",12 " Kumisasa kwabuka matenda a maso, mphere Nyumba zawo zudagwa, minda idakokoloka ndipo katundu wambiri kuphatikizapo ziweto zidanka ndi madzi osefukira. Anthu miyandamiyanda, maka akuchigwa cha Shire, adathawira kumtunda kuti apulumutse miyoyo yawo, koma komwe adathawirako nakonso kwaopsakwagwa mliri wa matenda amaso ndi mphere mmisasa ya ku Nsanje ndi Chikwawa. Mneneri wa unduna wa zaumoyo Henry Chimbali watsimikiza izi, koma wati unduna wake ukufufuzabe za anthu amene akhudzidwa ndi matendawa. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Msasa wa Bitirinyu kwa T/A Nyachikadza mboma la Nsanje ndiwo wakhudzidwa kwambiri ndi matenda a mphere pamene misasa ya Bereu ndi Kalima kwa T/A Maseya mboma la Chikwawa ndiwo watekeseka ndi matenda a maso. Msasa wa Bitirinyu ukusunga anthu pafupifupi 6 000. Pamene Tamvani idazungulira pamsasa wa Bereu ambiri adali koyenda koma mayi Elube Jeke wa mmudzi mwa Chikutireni adali pamalopo akutonthoza ana ake. Mwana wamngonoyu wayamba kumene [kudwala maso] pamene wamkuluyu ndiye adayamba masiku atatu apitawo. Sakupeza bwino, maso atupa komanso akumadandaula kuti akumva kuwawa. Akapeza mtendere ndiye kuti wagona. Sitinalandirepo thandizo chiyambireni matendawa, zomwe zachititsa kuti pakhale kupatsirana, adatero Jeke uku akufunditsa mwana wokulirapoyo amene ati sakupita kusukulu chifukwa cha mavutowo. Mavuto sakukata kwa Jeke chifukwa pamene amabwera pamsasawo nkuti nyumba yake itagwa ndi madzi a mvula ndipo katundu wake limodzi ndi munda zidakokoloka. Poti athawitse moyo, lero wakumana nazonso pamene matenda agwera ana ake. Sindingakhalenso ndi lingaliro lobwerera kumudzi chifukwa kumenekonso ndiye sikuli bwino. Madzi sadaphwere, adatero Jeke, kusowa mtengo wogwira. Mkulu woyanganira za umoyo pa msasawu, Rodrick Rivekwa, akutsimikiza za matendawa ndipo wati pofika Lachisanu pa 13 March nkuti anthu 15 atapezeka ndi matendawa. Iye adatinso anthu 10 ndiwo apezeka ndi mphere pamsasawo. Koma boma lachitapo machawi pofuna kuthana ndi vutoli. Adatitumizira mankhwala moti anthu onse amene akudwala maso ndi mphere alandira thandizo lachipatala, adatero Rivekwa. Iye adati kuchulukana kwa anthu pamsasa wa Bereu lingakhale vuto lina lomwe ladzeetsa mavutowo. Tili ndi anthu 1 024, koma malo ogona adali ochepa. Komanso kupeza madzi ndi aukhondo lidali vuto lina. Panopa bolako chifukwa atipatsa zipangizo zosungiramo madzi komanso matenti adationjezera, adatero Rivekwa. Nakonso kumsasa wa Kalima mavuto a matenda amaso sadasiye, malinga ndi John Yobe wa mmudzi mwa Kalima kwa T/A Maseya mbomalo. Yobe adathawa mmudzi mwake ndi kukakhala nawo kumsasawo. Iye akuti adali ndi ziweto monga nkhuku, mbuzi ndi nkhumba zomwe zidatengedwa ndi madzi. Pokakhala pamsasawu akuti amati ndi chisomo ndipo ankaganiza kuti wapulumuka, koma mwadzidzidzi adadabwa kuona ana ake asanu ndi mmodzi atagwidwa ndi nthenda ya maso. Yobe akuti pano zinthu zasinthako chifukwa thandizo la chipatala lidafika mofulumira ndipo nthendayi ati sidafale kwambiri monga amaopera. Malinga ndi nyakwawa Katandika, matendawa adza chifukwa chothithikana pamsasawu, zomwe anthuwa akhala akudandaula. Koma Chimbali adati unduna wake wafika kale mmalowa kukapereka thandizo la chipatala ndipo zinthu zikusintha. Talandiradi malipoti okhudza matenda a maso. Ambiri amene akhudzidwa ndi matendawa ndi ana. Msasa wa Bitirinyu kwa T/A Nyachikadza ndiko talandira malipotiwa. Koma zinthu zasintha chifukwa thandizo lapitako, adatero Chimbali. Iye adatinso mavutowa amveka mmaboma a Chikwawa ndi Nsanje kokha pamene mmaboma ena monga Thyolo ndi Mulanje komanso ku Balaka kulibe nkhaniyo. Mneneriyo adatinso matenda otsekula mmimba abukanso mmisasayi koma unduna wawo wapereka kale thandizo. ",6 " Anatchezera Sagona mnyumba Anatchereza, Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndili ndi zaka 20 ndipo amuna anga sagona mnyumba ndiye chonde, ndithandizeni. Akuti ndikawauza ankhonswe banja langa litha. Ukwati tapanga chaka chatha. Ndine A Blantyre Zikomo A, Mwamuna wakoyo ngwachibwana zedi! Mwangokwatirana kumene ndipo ukuti sagona mnyumba, ndiye amakagona kuti? Ukapanda kusamala naye ameneyo akugwetsa mmavuto aakulu-ndikunenatu matenda oopsa, kuphatikizapo HIV/Edzi. Ngati wayamba kale kunena kuti ukakanena kwa ankhoswe banja lithapo ndiye kuti iye za banja alibe nazo ntchito koma kusangalatsa chilakolako cha thupi lake basi. Ndiye usazengerezepo apa, pita kaitule nkhaniyi kwa ankhoswe, umve zimene anene. Ngati akufuna kuti banjali lithe, lithe basi. Mwamuna wachimasomaso ndi woopsa kwambiri ndipo safunika kumusekerera. ",12 " Kuchoka kwa Phoya kutisokoneza, atero ena Anthu mmadera osiyanasiyana msabatayi ati kuchoka kwa phungu wa chipani cholamula cha DPP mdera la ku mmawa mboma la Blantyre, Henry Phoya kwasiya mafunso ambiri mmitu yawo zomwe ati zingawasokoneze podzavota mchaka cha 2014. Anthuwa ati kuchokako kukusonyeza kuti kuchipani cholamula kwavunda zomwe ati zawachititsa kakasi kuti aone komwe angadzaponye voti yawo. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Koma katswiri wa za mbiri ya kale, Chijere Chirwa wati andale amachokachoka mzipani zawo kapena kuyambitsa chipani chawo kotero izi sizikuyenera kusokoneza anthu. Iye adati kuchoka kwa Phoya ukhale mwayi wa chipani cha DPP kuti apeze anthu ena atsopano omwe angamange chipanicho. Phoya Lachiwiri adalengeza kuti walowa chipani cha MCP. Iye adalengeza izi pa msonkhano wa atolankhani omwe udachitikira kunyumba ya mtsogoleri wa chipanichi, John Tembo. Pomwe Phoya amalengeza nkhaniyi, wachiwiri kwa mneneri wa chipani cha UDF, Ken Msonda adalengeza kuti wasiya ndale ndipo akukalera ana. Mmodzi mwa anthuwo, Florence Kamvamtope wa mmudzi mwa Kanyumbaaka kwa T/A Nsamala mboma la Balaka wati kuchoka kwa Phoya kupita kuMCP kukulozera kuti pena pake paola ku DPP polingalira kuti Phoya adali msalamangwe kuchipaniko. Sitinganene kuti kupita ku MCP kungabweretse chitukuko. Izi zingotisokoneza mavotedwe chifukwa tikusowa chipani chomwe tingachione ngati chithandiza, adatero Kamvamtope. Ndipo Frank Chibambo wa mmudzi mwa Chibwana kwa T/A Chikulamayembe mboma la Rumphi adati izi zikuonetsa kuti ku DPP kwaipa. Apa pakuoneka kuti pali chikaiko kuchipani cholamula zoti iwo amalimbikitsadi ufulu wa demokalase. Zikundipatsa nkhawa kuti kodi zikhala zolongosoka? sakukhulupirira Chibambo. Koma Chirwa akuti munthu akatuluka chipani, chipanicho chikuyenera kutengerapo mwayi, pounguza ndi kupeza anthu omwe angapititse patsogolo chipanicho. Phoya adachotsedwa kuchipani cholamula ndiye ali ndi ufulu kupita kuchipani chilichonse nthawi yomwe adatsutsana ndi lamulo loletsa kutengera chiletso boma ndi ogwira ntchito mboma. Tikatengera demokalase padalibe cholakwika chifukwa ngakhale uli kuchipani cholamula utha kumaperekerabe maganizo osemphana ndi ena, adatero Chirwa. Koma poyankhapo, Phoya wati anthu asadandaule chifukwa adziwa zoona zake posakhalitsapa. Sitikuvota mawa, ndiye tikhala tikulankhula ndi anthuwa kuti adziwe zingapo. Ndigwira ntchito yomwe akufuna. Ngati boma lingabwere ndi mabilu ena omwe sakomera Amalawi tiona kuti tithana nawo bwanji. Aboma akabweretsa zokomera anthu tiwathandiza koma ngati zikhale zosakomera anthu ndiye zioneka, adatero. Phoya adali phungu kuchipani cha UDF mu 1999 mpaka 2004 ndipo adakhalapo nduna muulamulirowo. Iye adalowa hipani cha DPP ndipo adakhalaponso nduna muulamuliro wa chipanicho. ",11 " Ulendo wa chisankho wapsa Zipani zina zati bungwe loyendetsa chisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) liyenera kukwaniritsa zomwe lidalonjeza sabata yatha kuti chisankho cha 2019 chidzayenda mosakondera mbali. MEC idakhazikitsa ulendo wa chisankho chimene chidzakahalepo pa 21 May 2019 ndi lonjezo limodzi: Palibe kukondera. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Wachiwiri kwa mlembi wamkulu wa chipani cha Malawi Congress (MCP) Eisenhower Mkaka adati lonjezo lotereli limanenedwa nthawi zonse kumayambiriro kwa ulendo ngati kuno koma pamapeto pake zimaoneka ndi zina. Tili ndi chikhulupiliro kuti ulendo uno, MEC isunga lonjezo lake ndipo tiziyanganira kuti lonjezoli akulikwaniritsa motani? Vuto ndiloti timamva lonjezo lomwelomwelo nthawi zonse koma kumapeto timaona zina, adatero Mkaka. Mneneri wa chipani cha Peoples Party (PP) Noah Chimpeni wati nkhawa yawo ili pakusasunga lonjezo kwa bungwe la MEC lomwe nthawi zambiri limawoneka kuti limapereka mpata waukulu ku mbali ina. Nthawi zonse amatero koma sitidaonepo umboni oti akwaniritsa lonjezoli. Ngati akunena za chilungamo, ndiye awonetsetse kuti chipani chilichonse chizikhala ndi mpata ofanana ngakhale pa MBC osati olamula okha ayi, adatero Chimpeni. Iye adati pakhalenso ndondomeko yoonetsetsa kuti aliyense azikhala ndi mpata wa msonkhano kulikonse komwe wafuna chifukwa nthawi zina misonkhano ina amayiletsa nthawi yothaitha ponena kuti kumaloko kukupita mtsogoleri wa dziko. Chipani cha United Democratic Front (UDF) chati aka sikoyamba chipanichi kumva lonjezo lotere kuchokera ku bungwe la MEC koma chomwe chimavuta nkukwatitsa lonjezoli ndi zochitika. Mneneri wachipani cha UDF Ken Ndanga adati chipani chawo chimafuna ntchito zooneka ndi maso osati mawu chabe. Sikoyamba kumva mawu amenewa kuchoka pakamwa pa MEC. Zakhala zikunenedwa koma chimavuta nkukwaniritsa mawuwo. Nkhani yaikulu ndi ntchito osati mawu chifukwa anthu timakhala tikuona zochitika, adatero Ndanga. Mlembi wamkulu wa chipani cha Alliance For Democracy (Aford) Christopher Ritchie wati chipani chawo chitsatira ndondomeko zomwe MEC yakhazikitsa koma nacho chiyembekezera MEC kukwaniritsa mbali yake monga mwa lonjezo. Paliponse pamafunika chilungamo kuti zinthu ziyende bwino ndipo ife a Aford timakhulupilira chilungamo. Choncho, titsatira ndondomeko koma nawonso akwaniritse zomwe alonjeza osati tidzawone zina kumapeto, adatero Ritchie. MEC idatsegulira ulendowu pa 20 February 2018 ndipo zipani za ndale zati kupatula zokonzekera zina ndi zina, maso awo ali pa lonjezo lomwe bungweli lidapereka kuti chisankhocho chidzakhala chopanda zitopotopo. Wapampando wa MEC Jane Ansah adalonjeza kuti chisankho cha 2019 chidzakhala chokomera aliyense chifukwa bungwelo lilibe mbali iliyonse yoti mwina ena azikayika kuti pangadzakhale kukondera. Bungwe la MEC ndilodzipereka kuchititsa chisankho cha mtendere ndi chokomera aliyense. Paulendo onse mpaka kumapeto, pakhala chilungamo ndi kuika zinthu pamtetete ndipo sitidzasekerera ogwira ntchito ku MEC aliyense opanga zautambwali, adatero Ansah. Iye adati bungwelo likuyembekezeranso mgwirizano kwa onse okhudzidwa ndi chisankho chomwe chikudzachi ndipo kuti zikatero, nalo (bungwe la MEC) lidzayesetsa kuti lisaopsezedwe kapena kutumidwa ndi mbali kapena mphamvu iliyonse. Ansah adati makomo a MEC akhala otsegula paulendo onse ndipo bungwelo lidzalandira ndi kuchitapo kanthu pa dandaulo lililonse lomwe okhudzidwa angadzabweretse mosaona nkhope. Koma zipani zina za ndale zati zamva lonjezoli koma maso ake akhala akuyanganitsitsa pa MEC kuti zione komwe lonjezoli lizilowera mpaka komwe likathere. Bungwe loona za kayendetsedwe ka ndale za zipani zambiri la Centre for Multiparty Democracy (CMD) lati paulendowu mpofunika kugwirana manja pakati pa mbali zosiyanasiyana kuti tikafike bwino. Wapampando wa bungwelo Kandi Padambo adati magulu monga zipani za ndale, nyumba zofalitsa nkhani ndi boma makamaka oyanganira thumba la chuma akuyenera kutengapo mbali kwambiri. Ku mbali ya boma, mpofunika kupereka ndalama zoyendetsera chisankho zokwanira nthawi yabwino, adatero Padambo. ",11 " Woganiziridwa kuba khanda anjatidwa ku Mzuzu Mayi wina zake zada mumzinda wa Mzuzu atamugwira ataba khanda la psuu la mnzake pachipatala chachikulu cha Mzuzu sabata yatha. Koma make mwanayo pano akumwetulira chifukwa khanda lakelo lilinso mmanja mwake! Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Wachiwiri kwa mneneri wa polisi ya Mzuzu, Cecelia Mfune, watsimikiza za kumangidwa kwa Mary Pundi Nyirenda, wa mmudzi mwa Chisi, T/ A Mpherembe mboma la Mzimba, yemwe akumusunga palimandi kundende ya Mzuzu komwe akudikirira kukaonekera kubwalo la milandu komwe akayankha mlandu woganiziridwa kuba khanda masiku akubwerawa. Alinso limodzi: Wayisoni ndi mwana wake atapezeka Komatu khandali likadapita pakadapanda Maganizo Banda, mlonda wa kampani ya Stallion, yemwe ankalondera malowa usikuwo. Banda adati adakhala tcheru ataona Nyirenda akutuluka ndi khanda kuchokera muwodiyo nthawi itatsala pangono kukwana 12 koloko usiku. Mayiyu adatuluka katatu konse kulowera wodi ya amayi apakati, yomwe ili moyandikana kwambiri ndi wodi ya makandayi, atanyamula khanda lomwe adalikulunga mushawelo yoyera. Amati kutuluka nkulowa. Apa ndidadziwa kuti china chake chasokonekera chifukwa kunja kudali kukuzizira ndipo mayi wanzeru sakadatuluka ndi mwana nthawi ngati imeneyo ndipo sindidamulole kuti atuluke, adatero Banda. Pocheza ndi Msangulutso make khandalo, Mercy Wayisoni, wa zaka 27 yemwe amachokera ku Elunyeni mboma lomwelo koma kumudzi kwawo ndi kwa Nazombe, T/A Nazombe mboma la Phalombe, adafotokoza kuti adafika pachipatalapo Loweruka pa February 20 wopanda wina aliyense womudikirira. Iye adati Loweruka lomwelo adakumana ndi mayi wina kukhitchini yemwe adamufunsa ngati ali ndi womudikirira ndipo iye atamuuza kuti adalibe aliyense womusamalira pachipatalapo, mayiyo adamupempha kuti akhale mnzake kuti aziphika ndi kudya limodzi osadziwa kuti adali zolowere nkudyere mwana. Apa mpomwe ubwenzi wathu udayambira. Kwa masiku asanu ndi limodzi tinkadyera limodzi, adatero Wayisoni koma adati adadabwa kuti Lolemba nthawi yochira itakwana Nyirenda adamuletsa kuitana wachibale aliyense kuti amuthandizire ndipo adamuuza kuti wachibale aliyense asadziwe zoti nthawi yake yochira idali itakwana kaamba koti iye alipo ndipo amuthandiza. Wayisoni adati Nyirenda adali kumutsatira kulikonse komwe amapita patsikuli mpaka kuchipinda cha opaleshoni komwe adanamiza adokotala kuti adali wolandirira mwana ngakhale adokotalawo adamuletsa kulowa mchipindamo. Iye adati asadatuluke kuopaleshoniko, adokotala adamudziwitsa kuti adali ndi mwana wamwamuna. Wayisoni adati adazizwa pomwe adadzidzimuka pakati pa usiku ndi kupeza kuti mwana wake salinso kumtima kwake koma mnzakeyo adali atamusunthapo. Adandiletsa kumuyangana mwana wanga ndi kundiuza kuti khandalo silidali langa koma lake kaamba koti langa lidapitirira. Izi zidandikwiyitsa ndipo ndidauza oyandikana nawo kuti Nyirenda wanditengera mwana ndipo adasinthitsa nsalu ine ndili mtulo, adalongosola Wayisoni. Iye adati nawo achipatala atamva kuti muwodimo mwauka mpungwepungwe adabwera ndi kutsimikiza kuti khandalo lidali la Wayisoni. ",7 " Chilimikani pa ulimiKazembe Malinga ndi ngamba imene yasautsa mmadera ambiri mdziko lino, wachiwiri kwa kazembe wa limodzi mwa maiko a ku Ulaya la Flanders, Nikolas Bosscher wati boma la Malawi liyenera kuika mtima potukula ulimi mdziko muno. Bosscher adanena izi Lolemba pa msonkhano wa dzidzidzi wa komiti ya National Agricultural Content Development Committee (NACDC). Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Iye adati kuti dziko lino lithane ndi mavuto akudza chifukwa cha kusintha kwanyengo, nkofunika kubweretsa chitukuko chachikulu kumbali ya ulimi. Dziko la Malawi silikuchita chitukuko chenicheni kumbali ya ulimi chifukwa ndalama zambiri zikumapita kundondomeko yopereka zipangizo zaulimi motsika mtengo ndi kugula chimanga zomwe sizingamange maziko olimba otukula ulimi, adatero iye. Iye adati ulimi ukumakhudzidwa ndi china chilichonse chokudza monga ngamba, tizilombo toononga mbewu, matenda ngakhale kusowa kwa misika kumene. Choncho boma liyenera kuika patsogolo ndikubweretsa chitukuko kumbali ya ulimi. Monga madera omwe chimanga chaumiratu, mlimi ayenera kuuzidwa kuti azule chimangacho ndikubzala mbewu zina monga chinangwa ndi mbatata, adalongosola Bosscher. Mkulu wa nthambi ya ulangizi ku unduna wa zaulimi Jerome Nkhoma yemwe adali nawo pa msonkhanowo adati boma laika kale mtima pa chitukuko ndipo mwazina lidaika mlozo womwe kampani zingatsate pobweretsa chitukuko kumbali ya ulimi. Nkhoma adati nkofunika kuti alimi apatsidwe uthenga oyenera mwachangu okhudzana ndi ulimi pothana ndi vutoli. Ndipo Farm Radio Trust, bungwe lomwe limathandiza kufalitsa uthenga kwa alimi, yomwe idaitanitsa msonkhanowo idati zinthu sizili bwino mdziko muno ndipo alimi ambiri akhudzidwa ndi ngamba ndi mbozi zomwe zikuononga mmera. Ngakhale tidauzidwa kuti kukhala ngamba komanso mbozi zoononga mmera, sitimayembekezera kuti vutoli likhala lalikulu chonchi, adatero George Vilili wochokera ku bungwelo. Pomwe mkulu wa nthambi yoona zanyengo Jolamu Nkhokwe adati nthambi yake idanena kuti chaka chino kukhala ngamba komanso madzi osefukira mwezi wa September chaka chatha. Nkhokwe adati mvula ikadali kugwa, ndipo Madera ena omwe mudagwa ngamba, alandira mvulayi komabe adalimbikitsa alimi kutsatira uthenga omwe nthambi yake imapereka nthawi ndi nthawi. ",4 " Akufuna chakudya ku Nsanje Ngakhale maboma ambiri zikuoneka kuti apata chakudya mnyengo ya ulimi yangothayi, anthu ena mboma la Nsanje ati akufuna thandizo la chakudya lomwe mabungwe ndi boma amapereka lipitirire kwa miyezi ina itatu chifukwa sanakolole chimanga chokwanira ndipo ali pa njala. Phungu wa dera la kummwera kwa bomali, Thomson Kamangira, adanena izi pamsonkhano wa chitukuko omwe nduna yofalitsa nkhani Nicholas Dausi idachititsa podziwitsa anthu pulojekiti ya boma yoonetsetsa kuti netiweki ya lamya ikupezeka mmaboma onse mosavuta yotchedwa Malawi National Fibre Backbone sabata yatha. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Dausi: Tiyesetsa anthu asafe Kamangira adati ngamba yomwe inagwa chimanga chitangomasula ngayaye inasokoneza mbewu mbomalo. Tikusowa zambiri koma pakali pano vuto ndi la njala. Izi ndi kaamba ka ngamba osati madzi osefukira. Mabungwe asiya kupereka chakudya, koma tikuwapempha kupitiririza kwa miyezi itatu kuti tipulumuke ku njala yomwe itisause posachedwapa, adatero Kamangira. Pothirira ndemanga, khansala Robert Chabvi adati anthu mderalo chaka chinonso zawavuta kumunda ndipo boma ndi mabungwe awapase zida zochitira ulimi wamthirira. Sikuti ndife opemphetsa koma chimanga chatilakanso chaka chino. Boma ndi mabungwe tipatseni zida za ulimi wamthirira zoyendera mphamvu ya dzuwa kuti tilimenso uku mukutipatsa thandizo la chakudya. Pokhala kumudzi, anthu alibe chuma chogulira chimanga kwa mavenda kapena ku Admarc, adatero Chabvi. Poyankhapo, Dausi adati anthu asadere nkhawa chifukwa mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika achita zotheka kuti aliyense asafe ndi njala. Izi zikusemphana ndi lipoti la boma la mu February lomwe linati chimanga chikololedwa chochuluka matani 3.2 miliyoni kusiyana ndi chaka chatha 2.3 miliyoni. Malinga ndi mkulu wa Farmers Union of Malawi (FUM) Alfred Kapichira Banda nzosadabwitsa kuti anthu ena ku Nsanje adandaule za njala. Zolosera pa zokolola sizimasonyeza momwe zinthu zilili, adatero iye. ",6 " Richard Mbulu: Chilombo cha Mafco FC Dzina la Richard Mbulu lasanduka nyimbo ya mizinda yonse chifukwa cha ntchito zake zomwetsa zigoli. Pano Mbulu akutsogola mu TNM Super League ndi zigoli 11, adamwetsanso zigoli 17 mu Presidential Cup. Kodi Mbulu ndani? BOBBY KABANGO akucheza naye. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mbulu: Chilombo pankhani yokankha chikopa Wawa Mbulu Mbuluyo ndiye ineyo, mani. Kodi ndi Mimbulu? Kapena Mbulu basi? Ndine Mbulu, koma dzina limeneli likuchokera ku dzina loti Mimbulu, tinyama tovuta kwabasi. Ndiye iwe ndiwe wovuta? Kumbali ya mpira basi, kuvuta kwanga ndi kumeneko, koma zinazi ndiye ndine munthu wabwinobwino. Timudziwe kuti Mbulu ndani? Mbulu ndi ineyo, mnyamata wochokera ku Mangochi, woyamba kubadwa mbanja la ana asanu. Mbiri yako pachikopa ndiyotani? Poyamba ndimasewera ku Navy FC kapena kuti Marine MDF, nditachoka kumeneko, ndidakatera ku [Big] Bullets komwe ndidakhalako kwa miyezi iwiri. Ku Navy ndidachokako nditangolemba mayeso a Form 4 mu 2013. Zidayenda bwanji ku Bullets? Sadandipatse mwayi woti ndisewerere mtimuyo, panthawiyo amati ndine mwana. Ndidachoka ulendo ku Mafco FC komwe adandilandira bwino. Chipitireni ku Mafco wachinya zingati? Ndachinya zigoli 108 za ligi ndi makapu omwe, apatu ndikutanthauza kuyambira 2013 mpaka lero. Mphekesera zikuti mwayi wapezeka wokasewera ku Baroka FC ku Joni, ndi zoona? Zili choncho koma sindingayankhe zambiri pankhaniyi. Ineyo ndine msirikali ndiye oyenera kuyankha pankhani imeneyi ndi mabwana anga. ",16 "Wachitetezo wa Mutharika; Chisale Wamangidwa Apolisi amanga yemwe anali wamkulu wa achitetezo kwa mtsogoleri wakale wa dziko lino Peter Mutharika, a Norman Paulos Chisale. Ali mmanja mwa apolisi-Chisale (wavala jekete ya blue) Wofalitsa nkhani za apolisi mdziko muno, James Kadadzera watsimikiza za nkhaniyi polankhula ndi Radio Maria Malawi. Ndizoona kuti ali mmanja mwathu kuno ku Lilongwe maka maka ofesi yofufuza fufuza nkhani yokhuza chuma. Ife apolisi timayitana anthu omwe tikuwaganizira pa nkhani inayake ndi kumawafusa kudikira kuti tipeze umboni weni weni,anatero Kadadzera. Kadadzera: Tinenabe zifukwa zomwe tawamangira Malipoti akusonyeza kuti a Chisale amangidwa pokhudzidwa ndi nkhani yolowetsa cement mdziko muno opanda msonkho. Koma mneneri wa apolisiyu wakana kunena zifukwa zomwe awamangira a Chisale ponena kuti akufufuzabe. ",7 "Papa Apempha Akhristu Apempherere Msonkhano wa ma Episcope ku Amazon Wolemba: Sylvester Kasitomu Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisko lamulungu wapempha akhristu a mpingo-wu pa dziko lonse kuti apemphere ma Episcope a mpingo-wu ndi adindo ena ku Amazon omwe ayamba kuchita msonkhano wawo wa sinodi. Papa Francisco walankhula izi ku likulu la mpingo-wu ku Vatican. Iye wafuniranso zabwino atsogoleri ndi adindo ena omwe akuchita nawo msonkhano-wu, ndipo wapempha ma episcopi-wa kuti pomwe akuchita msonkhano-wu awonetsetse kuti agunda ndi kukambirana mfundo zabwino zomwe zingathandize pa ntchito zokweza mpingowu mu sinodi-yo. Iye wapereka pempholi patangopitanso miyezi yochepa pomwe dziko la Brazil lakhala likumana ndi ngozi ya moto pomwe nkhalango yayikulu ya Amazon yomwe mbali yaikulu iri mdzikoli inatenthedwa zomwe zinachititsa kuti zachilengedwe zambiri zionongeke. ",13 " Wezzie: Chiphadzuwa chonenepa cha Mzuni Sukulu yaukachenjede ya Mzuzu University idasankha chiphadzuwa chonenepa Loweruka sabata yatha pomwe adali ndi chisangalalo chawo cha Social Weekend. Mtolankani wathu DAILES BANDA adacheza naye motere: Tikudziweni Chisale watuluka nkumangidwanso Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Ndine Wezzie Lwara ndipo ndimachokera mmudzi mwa Thom Lwara, kwa Inkosi ya Makhosi Mmbelwa mboma la Mzimba. Kwathu tinabadwa ana awiri ndipo ndine woyamba kubadwa. Ndili ndi zaka 20. Manthu wa ziphadzuwa: Lwara (pakati) ndi omutsatira ake Mbiri yako ya maphunziro ndi yotani? Ndidalemba mayeso anga a Fomu 4 pasukulu ya sekondale ya Ekwendeni, padakalipano ndikuphunzira zokopa alendo pa Mzuzu University. Ndili chaka chachiwiri. Udayamba liti za uchiphadzuwa? Kunena chilungamo aka nkoyamba kuchita izi. Mnzanga wina adangobwera kudzandiuza kuti ndikayese ndipo ndikhoza kupambana. Kuyesera ndi kupambana kudali komweko. Udazilandira bwanji za kupambana kwako? Sindikuchitenga chinthu chapafupi chifukwa sindidakonzekera kwambiri monga anzanga adachitira. Ndine wosanglala kwambiri makamaka chifukwa cha mphatso yomwe ndidalandira ya ndalama zokwana K50 000. Ndiye ukuwauza chiyani makolo ako? Kusukulu ya ukachenjede ndi komwe anthu amaphunzira ndi kuchita zinthu za msangulutso zambiri. Iyi ndi nthawi yomwe aliyense amene adapitako kusukuluzi amakumbikira kuti adasangalala. Atsikana uwalangiza zotani? Azilimbikira sukulu kuti adzafike malo ngati ano ndipo asamakhale ndi mtima odziderera. Pa atsikana amene tidapikisana, sikuti pasukulu pano atsikana onenepa ndife tokha ayi koma kumakhala kudzikaikira komwe kumatilepheretsa kuchita zinthu. ",15 " Akangalika ndi ulimi wa mthirira Mlimi wochenjera monga NELLIE NYONI wa mboma la Balaka amayambiratu ulimi wa mchilimwe mvula ikamapita kumapeto kuti asavutike kwambiri ndikuthirira. Tikunena pano adabzala kale chimanga komanso nyemba ndipo posachedwapa ziyamba kubereka. ESMIE KOMWA adacheza ndi mlimiyu motere: Ulimi wa mchilimwe umaposa wa mdzinja Kodi nchifukwa chiyani mumafulumira kuyambapo ulimi wa mthirira? Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Choyambirira ndimafuna kuti ndigwiritse ntchito chinyezi chochuluka chomwe chimapezeka mvula ikangosiya kugwa kuti mbewu zikamadzafuna madzi owonjezera ndidzangothirira kanthawi kochepa basi zatheka. Chifukwa china nchoti ndimafuna ndizipezeka ndi mbewuzi pafupipafupi kuti ndizipeza phindu lochuluka. Nanga mudayamba liti ulimi wa mthirira? Ulimiwu ndidayamba mu 2004. Kodi chidakukopani pa ulimiwu nchiyani? Ndidaona kuti mbewu za mthirira zimagulitsidwa pa mtengo kusiyana ndi zodalira mvula ndipo ichi nchifukwa chomwe ndimazilimbikira. Nanga mumalima mbewu zanji? Ndimalima mbewu zosiyanasiyana monga tomato ndi kabichi koma kwambiri ndimaonjeza chimanga. Kodi mumalima mbewuzi pamalo okula bwanji? Malo womwe ndimachitirapo mthirirawu ndi wokwana ma ekala 6 ndi theka. Nanga zikayenda bwino mumapeza ndalama zochuluka bwanji pakamozi? Mbewu yomwe ndimaiwerengetsera bwino ndi ya chimanga chifukwa ndimailima mochuluka monga ndanena kale. Chimangachi chikakhwima ndikugulitsa chachiwitsi ndimatha kupeza K600 000 ndipo zikavutirapo K500 000. Kodi chinsinsi chanu chagona pati? Chinsinsi changa ndikusamalira mbewu kuti zichite bwino. Ndimaonetsetsa kuti zizipeza madzi wokwanira, ndimathira feteleza, ndimapalira komanso kuthana ndi zilombo zoononga kuti zichite bwino. Ubwino wa mbewu za mthirira ndiwoti zikangotheka ndimadziwiratu kuti zanga zayera. Kodi mumagwiritsa ntchito mthirira wanji? Kwa zaka zonsezi ndakhala ndikugwiritsa ntchito ma water cane kuthiririra mbewu zanga koma padakali pano ndagula pampu yopopera madzi yogwiritsa ntchito petulo. Nanga ndi mavuto anji omwe mumakumana nawo pogwiritsa ntchito mthirira woterewu? Kunena zoona mthirira wa mtunduwu ndiwopweka kwambiri. Tangoganizani kuti munthu ukwanitse kuthirira malo wokula motere sizamasewera koma khama langa pa ulimiwu ndilomwe limandichititsa kuti ndizilimbikirabe. Nanga ndi mavuto anji omwe mumakumana nawo pa ulimiwu? Vuto lalikulu ndikusowa kwa zipangizo za mthirira za makono zogwiritsa ntchito madzi ochepa. Vuto lina ndikusowa kwa madzi othiririra mbewu makamaka tikamayandikira nyengo yotentha zitsime zomwe timadalira nthawi zina zimaphwa ngati mvula siidagwe yokwanira. Izi zimachititsa kuti tidukize panjira nkumadikirira mvula mmalo moti tizilumikiza kwa chaka chonse. Chinthu chokhumudwitsa kwambiri nchoti ulimiwu timangozichitira popanda alangizi a mthirira ndipo ndimadabwa ngati alipo mdziko muno. Nanga masomphenya anu pa ulimiwu ndiwotani? Ndikufuna mtsogolomu nditaika mthirira wa makono uja amalumikiza mapaipi ndikumangotsegula madzi kuti azifikira mbewu okha. Mthirira woterewu umafuna mlimi akhale ndi matanki, zitsime zakuya ndi zopopera madzi zogwiritsa ntchito zipangizo zoyendera magetsi kapena mphamvu ya dzuwa. Izi zidzandithandizira kuti ndizitha kukhala ndi madzi kwa chaka chonse komanso kupopa mosavuta ndikumathiririra mbewu zanga. Kodi mudzapitiriza kulima mbewu zomwe mukulima panopazi? Ayi ndikufuna ndidzayambe ulimi wa kachewere chifukwa ndidamva kuti ndiwaphindu kwambiri koma ndimakanika kuyamba panopa chifukwa cha mavuto omwe ndanena aja. Kabitchi ndi mbewu ina yomwe ndimaganiza kuti ndidzaikirapo mtima. Nanga muchita chiyani kuti mukwaniritse masomphenyawa? Pa ine ndekha ndikuona kuti ndizovutirapo chifukwa zipangizo za mthirira wa mtunduwu ndizokwera ntengo kwambiri. Ndidakakonda padakapezeka mabungwe omwe akhoza kundithandiza kufikira masomphenyawa. Tidayetsera kuwafotokozera a ku nthambi yoona za ulimi wa mthirira koma adangotiyankha kuti tikuthandizani kutenga ngongole ku banki. Ngakhale adatilonjeza motere koma tikuona kuti izi sizingachitike choncho ndikupempha akufuna kwabwino kuti andithandize. ",4 "Phungu Adandaula ndi Kuchepa kwa Ndalama Zokonzera Miseu ya Mmizinda Wolemba: Sylvester Kasitomu a.mw/wp-content/uploads/2019/10/Jiya-170x170.jpg 170w"" sizes=""(max-width: 307px) 100vw, 307px"" />Jiya: Misewu yambiri ikufunika kukonzedwa Phungu wa dera la pakati mu mzinda wa Lilongwe Alfred Jiya wadandaula ndi kuchepetsedwa kwa ndalama zokonzera miseu ya mmizinda ya dziko lino. Phungu-yu wati ndondomeko ya za chuma ya 2019 mpaka 2020, boma laika padera ndalama zokwana 2.2 billion kwacha kuti zigwire ntchito yokonza misewu ya mmizinda ya Lilongwe, Blantyre, Zomba komanso Mzuzu zomwe wati ndi zochepa poyerekeza ndi mmene ntchito yomanga misewu imakhalira. Iwo ati ndi ntchito ya iwo monga aphungu kuonetsetsa kuti chaka ndi chaka pasakhale mavuto monga miseu ya mmizinda yomwe ndiyofunika kwambiri ndipo sikufunika kukhala yoonongeka. Pali miseu yambiri yoti simadusika nthawi ya mvula monga nseu wa masafu kupita pa zebra komanso wakumagwero kufika ku 23 ndi ina yambiri miseu yi ikufuna kukonzedwanso nde ngati achepetsa ndalama nde kuti akunena kuti miseu ikhalebe yoonongeka zomwe ndizokhudza kwambiri, anatero Jiya. Mwazina iwo ati ngati boma silichitapo ayesetsa kupeza njira yolikakamiza kuti lithandizepo poonetsetsa kuti misewuyi yakonzedwa nyengo ya budgetiyi isanadutse. ",17 "Papa Ayendera Odwala- Ali Mdziko la Thailand w"" sizes=""(max-width: 453px) 100vw, 453px"" />Papa pa chipatala cha St. Louis mdziko la Thailand Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko Papa Francisko anakayendera odwala pa chipatala cha St. Louis mu mzinda wa Bangkok pa ulendo wake omwe akucheza mdziko la Thailand. Polankhula ndi ogwira ntchito a pa chipatalachi okwana 700 iye anati ndi okondwa kuti anakayendera anthu pa chipatalachi omwe akusoweka thandizo makamaka la uzimu. Malipoti a wailesi ya Vatican ati chipatalachi anachitsegulira mu chaka cha 1898 ndipo mawu ake ochitsogolera ndi akuti Pamene Pali Chikondi, Mulungu Amakhalanso Pomwepo. Padakali pano chipatalachi chimayendetsedwa ndi madotolo, anamwino komanso ochita za kafukufuku ndi thandizo lochokera ku nthambi yoona za zipatala. ",14 " Maphunziro alowa nthenya Okhudzidwa ndi ngozi akuphuphabe Nthawi ili cha mma hafu pasiti leveni (11:30 am) ndipo kunja kukutentha koopsa. Ena mwa ophunzira pasukulu ya pulaimale ya Chikoja kwa mfumu Osiyana Mboma la Nsanje akuphunzirira pansi pamtengo wopanda masamba, ena ali mmatenti momwe mukutentha molapitsa. Ofesi ya aphunzitsi ili pansi pamtengonso umene masamba ake adayoyoka. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Posakhalitsa wophunzira wa Sitandade 4 wakomoka chifukwa chotentha ndipo ophunzira anzake akudzithira madzi kumutu pofuna kuziziritsa matupi awo. Awa ndiwo mavuto amene amanga nthenje pasukulu ya Chikojayi, yomwe idakhudzidwa ndi madzi osefukira. Nazonso sukulu za Chingoli mboma la Mulanje ndi Mvunguti mboma la Phalombe akukumana ndi zokhoma zokhazokhazi. Pamene patha miyezi 8 chichitikireni ngoziyi, nyumba za aphunzitsi, zimbudzi komanso mabuloko ndi maofesi a aphunzitsi sizidakonzedwe, zomwe zikupereka mantha kuti mavutowa angakhodzokere mvula ikayamba mwezi ukubwerawu malinga ndi azanyengo. Wachiwiri kwa mphunzitsi wamkulu pasukulu ya Chikoja, Clement Seda, akuti ngati mvula itayambe ndiye zivutitsitsa. Panopa tikupirira dzuwa, koma ngati mvula ikayamba ndiye palibe chabwino, sukulu idzatsekedwa kaye. Mboma la Nsanje, madzi osefukira adagwetsa sukulu ya Chinama ndi Namiyala. Izi zidachititsa kuti boma limange matenti kuphiri la kwa Osiyana kwa T/A Mlolo kuti ophunzira azikaphunzirirako pamene matenti ena adamangidwa kwa Chambuluka. Kumangidwa kwa matentiwa, chidali chimwemwe kwa aliyense kuti basi athana ndi mavuto osefukira kwa madzi, koma lero kwaipa pamene mavuto ena afika mkhosi. Seda akuti boma lidalonjeza kuti ayamba kuwamangira sukulu nthawi ya mvula isadayambe. Koma mpaka lero kuli chuu. Adatimangira matenti asanu ndipo makalasi ena akuphunzirira panja. Poyamba tinkadandaula ndi ana amene ankaphunzira panja, koma pano tikudandaulanso ndi matentiwa chifukwa mukutentha kwambiri. Mwaona nokha kuti mwana wina kuti Sali bwino, mavuto amenewa achulukira chifukwa matenda amutu si nkhani, adatero Seda. Seda adati aphunzitsi onse akukhala ku Fatima ndi Makhanga, womwe ndi mtunda wa makilomita osachepera 14. Tikafulumira kufika kuntchito ndiye kuti ndi 8:30 mmawa kusonyeza kuti piriyodi imodzi imadutsa tisanafike, komanso chifukwa chotentha, ophunzira amaweruka mofulumira dzuwa lisadafike powawitsa. Izi zikuchititsa kuti ana asaphunzire mokwanira, komanso ambiri sakubwera chifukwa cha mavuto amene tikukumana nawowa, adatero Seda. Iye adati izi zachititsa kuti zotsatira za mayeso a Sitandede 8 chaka chino zikhale zosokonekera. Mwa ana 40 amene adalemba mayeso a PSLC, ana 4 okha ndiwo adakhoza pomwe chaka chatha ana ana onse 35 adakhoza. Mu 2013 adalemba ana 85 ndipo onse adakhoza, mu 2012 ana 29 adalemba mayeso ndipo 27 ndiwo adakhodza. Sukuluyi yakhala ikuchita bwino kuyambira mmbuyo monse, adatero Seda, amene sukulu yake ili ndi ophunzira 900. Koma mneneri muunduna wa zamaphunziro Manfred Ndovi adati timupatse nthawi kuti afotokozepo zomwe boma likuchita kuti lipulumutse ophunzirawa. Nayo sukulu ya Chingoli pulaimale mboma la Mulanje akuti mavuto ndi ankhaninkhani malinga ndi DC wa mbomalo Fred Movete. Chimangireni matenti palibe chimene chachitikapo, mabuloko sadayambe kumangidwa moti zivuta kwambiri mvula ikayamba koma ndangomva kuti mapulani alipo kuti mabuloko amangidwa, adatero Movete. DC wa boma la Phalombe Paul Kalilombe akuti mbomalo mavutowa ndi ochepa kuyerekeza ndi maboma ena. Sukulu ya Mvunguti ndiyo idakhudzidwa, makalasi awiri okha ndiwo akuphunzira mmatenti koma ena ali mmabuloko, adatero Kalilombe. Maboma 15 ndiwo adakhudzidwa ndi ngozi ya madzi mu January chaka chino koma boma la Mulanje, Nsanje ndi Phalombe ndi omwe sukulu zidakhudzidwa. ",3 " Atukuka ndi kukwatitsa mitengo ya zipatso Masiku ano nkhani ili mkamwamkamwa paulimi ndi yogwiritsa ntchito mitundu ya mbewu zamakono zomwe akatswiri adayesa nkupeza kuti zili ndi kuthekera kotukula ulimi. Alimi a zipatso nawo adayambapo kutsata nzeruzi ndipo ena akusimba lokoma. Alimi a gulu la Taweni Farmers Club ku Mzimba akuchita nawo ulimiwu ndipo akudalira kwambiri kukwatitsa mitengo ya zipatso. Wapampando wa gululi Jester Kalua adafotokozera STEVEN PEMBAMOYO za ulimiwu motere: Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mlimi pantchito yake: Kalua kukwatitsa mitengo ya zipatso Bambo, dzina ndani? Dzina langa ndi Jester Kalua wa mmudzi mwa Kamanga kwa T/A Mtwalo ku Mzimba. Ndine wapampando wa gulu la alimi la Taweni Farmers Club. Kodi kalabu imeneyi mumapanga zotani? Ife timapanga ulimi wa zipatso zosiyanasiyana monga malalanje, mapapaya, mango, mapichesi ndi mapeyala. Tili ndi malo aakulu kwambiri omwe timabzalapo mitengo yazipatsoyi ndipo timathandizana kusamalira ngati gulu. Inu mumabzala mitundu yotani ya zipatsozo? Pali ntchito ndithu chifukwa sitimangofesa basi nkumayembekezera kuti tidzaokere, ayi. Pali zambiri zomwe timachita koma kwakukulu nkukwatitsa mitengo yathu yazipatso. Mukutanthauzanji mukatero? Ndikutanthauza kuti timatha kufesa mitengo ina yomwe sivuta kumera nkusamala panazale koma kenako timaikwatitsa ndi mitengo ina yomwe imabereka bwino koma imavuta kafesedwe kake. Kukwatitsako mumtani? Tikafesa mitengo yathu timayanganira mpaka itafika pamsinkhu wokwatitsa. Pokwatitsapo timadula nthambi ya mtengo womwe tikufuna kuti ukwatidwewo nkuikapo nthambi ya mtengo womwe tikufuna nkumanga. Tikatero timapitiriza kusamalira. Ndiye mtengowo sungafe? Ayi. Zomwe timachita nzakuti sitidula nthambi zonse koma mwina imodzi nkusiya nthambi zina zoti zizipanga chakudya cha mtengowo uku ukugwirana ndi unzakewo. Zikagwirana bwinobwino timatha kudzadula nthambi zinazo kuti mtengo wokhawo womwe tikufuna upitirire kukula. Cholinga chake nchiyani? Timafuna kupeza phindu lochuluka paulimi wathu chifukwa mbewu yomwe timaphayo imakhala yobereka pangono kusiyana ndi mbewu yokwatitsayo ndiye timafuna kupindulapo pa mbewu inayo. Mungatchuleko mitundu ya mbewu zomwe mukukwatitsa pakalipano? Tikukwatitsa mandimu ndi malalanje, mango achikuda ndi achizungu komanso mapichesi achikuda ndi achizungu. Ndiye mwati kusiyana kwake nkotani? Kusiyana kwake nkwakuti mbewu zachizunguzi zimabereka zipatso zikuluzikulu komanso zimabereka kwambiri kuposa mbewu zachikuda. Koma sindikumvetsa pakakwatitsidwe ka mandimu ndi malalanje. Nchifukwa chiyani mumapha mandimu kuti mudzakolole malalanje? Pali zifukwa zingapo. Choyamba mandimu savuta kafesedwe kake poyerekeza ndi malalanje ndiye timafuna kuti mandimuwo atiyambire moyo wosavutawo kenako nkuupatsira ku malalanje. Chachiwiri, mandimu ndi malalanje chili ndi msika waukulu ndi malalanje ndiye munthu aliyense akamabzala mbewu zodzagulitsa amaganizira za msika choncho ife timaona chanzeru kulimbikira malalanjewo. Mwanenapo za kasamalidwe, kodi mumasamala bwanji mitengi yanuyo? Zoonadi mitengo imafunika chisamaliro chokwanira bwino chifukwa kupanda kutero simungapeze phindu. Chiopsezo chachikulu ndi moto wolusa womwe umayamba mosadziwika bwino choncho mpofunika kulambula bwinobwino munkhalango ya zipatso. Kupatula apo mitengo sichedwa kugwidwa ndi matenda osiyanasiyana choncho pamafunika kuyendera pafupipafupi kuti ngati mwaoneka chizindikiro cha matenda, vutolo lithetsedweretu. Nthawi yokolola mumatani? Choyamba sitingokolola chisawawa koma pamakhala nthawi yake yokololera ndipo timayamba taona ngati zipatsozo zafika poti tikhoza kukolola. Timakana kungokolola chisawawa chifukwa zipatso zokolola zanthete zimabweretsa maluzi chifukwa maonekedwe ake zikapsa amakhala osapatsa chikoka. Inu misika yanu ili kuti? Tili ndi misika yosiyanasiyana ya zipatso. Zipatso zina timapikulitsa kwa mavenda ndipo zina timapita nazo mmagolosale akuluakulu omwe amatigulitsira nkumatipatsa ndalama. ",4 " Msika wa zondeni ngosayamba Katswiri wa zamadyedwe mdziko muno, Chrispine Jedegwa, akupanga ndi kugulitsa ufa wa mbatata ya kholowa yamakolo yotchedwa zondeni yomwe akuti ili ndi ufa wapamwamba wopatsa thanzi. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Anthu ambiri adazolowera kuti ufa umapangidwa kuchokera kuchimanga ndi chinangwa basi koma katswiriyu wati phindu lochokera mmbatata limachuluka mbatatayo ikagayidwa nkugulitsa ufa wake. Alimi ambiri sakonda kulima mbatata ya zondeni chifukwa sibereka kwambiri koma chomwe sadziwa nchakuti mbatatayi ili ndi mphamvu ya mankhwala ndipo muli ndalama zochuluka, adatero Jedegwa. Jedegwa: Ufa wa zondeni tikaukonza umakhala ngati uwu Iye adati mbatatayi ikacha ndipo mukaimuka bwinobwino mukaigaya mukhoza kupanga ufa wophikira phala kapena chakudya china chilichonse ndipo munthu akadya phalalo thupi lake limakulupala. Mkuluyu adati alimi alime mbatata ya mtunduwu kwambiri powatsimikizira kuti msika wake ulipo wosayamba. Pakalipano mbatatayi ikulimidwa kwambiri ndi alimi a ku Thyolo, Phalombe, Kasungu ndi Mchnji koma sakukwanitsa pomwe ife timafuna moti alimi omwe akufuna kupha makwacha alime mbatata yamtunduwu ndipo tikulonjeza kuti tidzawagula, adatero Jedegwa. Iye adatinso alimi atafuna mbewu ya mbatatayi yobereka kwambiri akhoza kukumana ndi akuluakulu a kampani ya C & NF omwe akupanga ufawu chifukwa mbewuyi alinayo yambiri. Alimi ambiri amadandaula kuti amalephera kulima mbewu zina polingalira nkhani ya msika koma Jedegwa watsimikiza kuti kampani yawo njokonzeka kugula mbatata yonse ya zondeni yomwe alimi angalime. Jedegwa adati kupatula kuti ndi chakudya, ufa wa mbatata ya zondeni ndi mankhwala othandiza kumatenda osiyanasiyana monga mtima, kuthamanga kwa magazi, shuga, zilonda zammimba ndi kuphwanya kwa minofu. ",4 " Kudali ku Presbyterian Church of Malawi Kudali kuphwanya mafupa ku Dream Centre Assemblies of God mumzinda wa Blantyre Loweruka pa 2 May pamene Faith Mussa amachititsa ukwati ndi bwenzi lake Brenda Chitika. Ndi kanamwali kopanda banga, kopanda chipsera. Thupi losalala komanso kathupi lomva mafuta. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ikokatu ndi ka mmudzi mwa Sikoya kwa T/A Chikumbu mboma la Mulanje. Iko ndi kachinayi kubadwa mbanja la ana asanu. Faith Mussa kuimbira namwali wake kanyimbo kachikondi Faith amene adatchuka kwambiri ndi nyimbo ya Desperate, akuti ubongo wake udasokonekera pamene adaona njoleyi Lamulungu mu 2009 pomwe mnyamatayu adapita kumpingo wa Brenda wa Presbyterian Church of Malawi (PCM) mumzinda wa Blantyre kukatsitsimuka. Faith adatsitsimuka zenizeni chifukwa kusalalanso kwa njoleyi kudaziziritsa mtima wake. Tsikuli Mulungu adakumana ndi chosowa chakedi. Ndili mumpingomo foni idaitana ndiye ndidapita panja kukayankha. Ndili panjapo kulankhula pa fonipo, ndidaona namwaliyu chapakataliko akutonthoza mwana, akutero Faith. Maso adali pa namwali, khuku lidali pa foni. Iye samasunthika ndipo pena Brenda akuti amathawitsa diso lake kuti asaphane maso ndi mnyamatayu koma Faith samasunthika. Izi zidatanthauza kanthu kena mumtima mwa Faith ndipo nkhani yonse idakambidwa patangotha mwezi. Titaweruka, ine ndi mchimwene wanga tidaperekeza namwaliyu. Ndinene apa kuti mwana amatonthozayo sadali wake. Poyamba Brenda amacheza ndi mbale wanga ndiye pamenepa ndidadziwiratu kuti ndikuyenera kuchita kanthu, adatero Faith. Pangonopangono awiriwa adakhazikitsa macheza ndipo Faith sadachedwetse koma kugwetsera mawu oti adzalumikize awiriwa kukhala banja. Padatha nthawi kuli zii, za yankho tidakayika koma pa 28 August 2009 ndidangolandira foni kundiuza kuti wagwirizana ndi [mbalume] zomwe ndidamuuza, adatero Faith wachiwiri kubadwa mbanja la anyamata atatu. ",13 " Tidadziwana tili ana Mtolankhani wa za masewero ku wailesi ya Voice of Livingstonia (VOL) Sylvester Siloh Kapondera adakumana ndi wokondedwa wake Annie Chivunga Kalasa ali ana mboma la Kasungu. Apatu nkuti Kapondera ali ndi zaka 11, mchaka cha 2001, ndipo ankacheza ndi achimwene a namwali wakeyu. Panthawiyo nkuti Kalasa naye ali wachichepere kwambiri. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ubwenzi wa anawatu udali bwino kwambiri chifukwa nawo makolo awo adali anansi pomwe onse ankaphunzitsa pa sukulu ya Mwimba, mboma la Kasungu. Siloh ndi Annisha: Zidayamba ngati chibwana Koma patadutsa zaka zingapo anthuwa adatayana pomwe adalowera malo osiyana. Koma mudali mchaka cha 2013 pomwe ndinkagwira ntchito kuwailesi ya Tigabane pomwe ndidayamba kumufuna namwaliyu! Panthawiyo nkuti akuchita maphunziro ake auphunzitsi ku Nkhamenya, mboma la Kasungu, adalongosola Kapondera. Iye adalongosola kuti atamuona Kalasa mtima wake udatumphatumpha mpaka kupempha nambala yake ya lamya yomwe adapatsidwa mosavuta chifukwa adali kale anansi. Nditabwerera ku Mzuzu ndidayamba kuchezetsa ndipo ndidamuuza mawu a chikondi komabe ndidakanidwa, ndidayesetsa koma zidavuta! Kenako kukhala ndekha kudandivuta ndipo ndidapeza mkazi wina! Komabe mtima wanga umakumbukirabe Annie! adatero Kapondera. Koma mwatsoka adasiyana ndi mkazi winayo ndipo Kapondera sadaupeze koma kubwerera kwa Kalasa komwe mtima wake udali. Nditasiyana ndi mkazi winayo kumayambirilo kwa 2017 sindidachedwe kupitaso kwa Kalasa komwe malingaliro anga adali! Apaso nayeso sadachedwe koma kundisekerera nkundilora ataona zoti sindimafuna kupanga naye chibwenzi wamba koma ubwezi woti timange banja, adalongosola Kapondera. Komatu ubwenzi wa awiriwa wakumana ndi zokhoma zosiyanasiyana monga kupekeredwa nkhani mwa zina. Chomwe chidandikopa kwambiri kwaiye ndichoti kupatula kuwala kwa namwaliyo, Ali ndi khalidwe lwabwino, ndi ofatsa komaso okonda kuseka moti sindimavutika kupeze nkhani yoseketsa kwambiri kuti mwina ndioneko mano ake, adatero Kapondera. Iye adati chikondi chawo chimalimba chifukwa chokhulupilirana komaso kulemekezana ndi kumvetsetsana! Polankhulapo, Kalasa adati adamukonda Kapondera chifukwa ankamuonetsera chikondi. Kalasa adati Kapondera amakondedwa ngakhale ndi abale ake. Ukwati wa awiriwa uliko pa April 28 kuholo ya sukulu ya sekondale ya Katoto. Kapondera ndi mwana wachiwiri kubadwa mbanja la ana asanu pomwe Kalasa ndi mzime mbanja la ana 6. ",15 " Tomato wabooka pa Bembeke Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Alimi ku Bembeke mboma la Dedza ayamba kufupa tomato wawo pamene wachoka pa mtengo wa K6 000 pa dengu kufika pa K1 000. Izi zikuchitika chifukwa cha kuchuluka kwa tomato amene akufika pamsikawu zomwe zachititsa kuti anthu opita ku Lilongwe kapena ku Blantyre azigula tomatoyu. Kutapa kutaya: Tomato amafunika kusamala Malinga ndi mmodzi mwa alimiwa, Akisa Magugu, mwezi wa March amagulitsa dengu pa mtengo wa K6 000 koma pano watsikiratu. Tikungofupa tomato, taganizani dengu lomwe timagulitsa K6 000 miyezi yangothayi lero latsika ndipo likupita pa mtengo wa K1 000 ndipo zikavuta akumagula pa mtengo wa K500. Taononga ndalama zambiri kuti tomatoyu tilime koma mapeto ake tangoyamba kufunano kwa anthu mopweteka kwambiri chifukwa tomato amene mumamuona pamsikawu sachoka pafupi, adatero Magugu. Kulira kwa Magugu mwina kungathe ndi ganizo lomwe mkonzi wa pulogalamu ya Ulimi wa Lero Excello Zidana, yemwe ndi mlangizi wa zaulimi, akunena: Vuto ndi alimiwa chifukwa amayamba kulima asadapeze msika. Ndi bwino alimi asadalime adziyamba aona msika momwe ulili komanso kumatchera nyengo yake chifukwa zimathandiza kuti idziwe nthawi yomwe mbewuyo imagulika bwino. Zidana akuti ndi bwinonso alimiwa aziyangana msika wina ngati zinthu zavuta choncho. Kuti upite madera ena upeza alimi akupha makwacha ndi mbewu yomweyo. Ayende misika ina ndithu akasimba mwayi, adatero. ",2 " Ndale zachibwana zalowa ku MCP Masapota a MCP sakudziwabe odzawatsogolera Kadaulo wa ndale kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College Blessings Chinsinga wati chipani cha Malawi Congress Party (MCP) chalowa chibwana, ndipo sichikudziwa momwe chingaongolere ndale mdziko muno. Chinsinga adanena izi Lachinayi potengera momwe chipanichi chikuyendetsera ndale pokonzekera chisankho cha 2014. Chipanichi chidalepheretsa msonkhano wake waukulu mu April ndipo masiku apitawa, chipanichi chidafuna kusefa ena mwa anthu 12 amene akufuna kudzapikisana nawo pampando wa yemwe adzaimire chipanichi pa chisankhocho. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Chipanichi chidakhazikitsa komiti younika anthu amene akufuna kudzapikisana nawo. Wapampando wa komitiyo ndi Lingson Belekanyama yemwe Lachitatu adati atakumana adapeza kuti sikofunika kuchotsa ena mwa omwe amafuna kudzapikisana nawo, makamaka amene sadakhale mchipanicho kwa zaka zisanu. Izi zimasonyeza kuti Lazarus Chakwera, yemwe adali mtsogoleri wa mpingo wa Assemblies of God, Felix Jumbe yemwe adali mkulu wa bungwe la alimi la Farmers Union of Malawi (FUM) komanso Lovemore Munlo yemwe adali mkulu wa majaji mboma la Bingu wa Mutharika sakadapikisana nawo pachisankhocho. Chinsinga adati chipanichi chikupereka unthenga osiyanasiyana okhudza tsogolo lake kwa Amalawi zomwe zikusonyeza kuti atsogoleri ake alibe mphamvu zowongolera kayendetsedwe kachipani. Msabata ziwiri zokha apereka mfundo zotsutsana zingapo. Choyamba mtsogoleri wawo John Tembo ndi mneneri wawo Jolly Kalelo adasemphana pankhani ya tsiku ndi malo a msonkhano wawo waukulu omwe anthu ambiri akuyembekezera. Sabata yomweyo Tembo adanena pawailesi ya Zodiak kuti achepetsa chiwerengero cha ofuna kudzapikisana nawo pampando wa odzayimilira chipanichi pa chisankho koma komiti yomwe imaunika anthuwo yati palibe kuletsa munthu kupikisana nawo, adatero Chinsinga. Iye adatinso sabata yomweyo, Tembo adauza nyuzipepala kuti adadzipereka kutsika pa mndandanda wa anthu ofuna kudzapikisana nawo pampandowo koma komitiyi yakana kuti palibe yemwe adadzipereka kutsika pamndandandawo. Apa zikusonyezeratu kuti palibe mgwirizano pakati pa akuluakulu achipani. Izi zikusonyezeratu kuti ndale zathu ndizosakhwima, adatero Chinsinga. Mmodzi mwa ofuna mpandowu mchipanichi Felix Jumbe, yemwe adali mkulu wa bungwe la alimi la Farmers Union of Malawi (FUM) adati amkhalakale ena a mchipanichi akupanga ndale zapansipansi pofuna kuipitsa anzawo. Chinsinga adati MCP ikulakwitsa chifukwa mmalo motsata ndondomeko zokhazikika za chipanicho, akubweretsa zachilendo zimene akuzikonza ndi anthu ochepa. Iye adati nzodabwitsanso kuti Tembo adakana kulandira K600 0000 yomwe Chakwera adapereka ku chipani ngati msonkha wake kuthumba lodzayendetsera msonkhano waukuluwo. Okha adanena kuti amene akufuna kudzapikisana nawo akuyenera kusonkha ndalama ndiye apa chokanira ndalama zina ndikumalandira zina ndi chiyani? Chofunika apa chipanichi chikuyenera kumapanga fundo zolimbitsa chipani, adatero Chinsinga. Tembo adauza atolankani kuti adakana ndalamazo chifukwa Chakwera adapereka nthawi yomwe akuluakulu a chipanichi amakumana kuti akambirane za mmene angachepetsere chiwerengero cha okufuna kutsogolera MCP. Iye adati kulandira ndalamazo kukadasokoneza ntchito yomwe amagwira akuluakuluwo poti Chakwera ndi mmodzi mwa anthu 12 omwe akufuna kudzalimbirana nawo mpandowo. Chakwera wati iye samapereka ndalama ku nkhumano wa akuluakuluwo koma kuthumba la ndalama zodzayendetsera msonkhano waukulu. Sindidatenge ndalama ndekha kukapereka. Ndidatsata ndondomeko yomwe idakhazikitsidwa kuti ndalama ziziperekedwa kudzera mwa anthu omwe akuthandiza chipani kutolera ndalama ndipo ine ndidachita chimodzimodzi, adatero Chakwera. Polankhula ndi wailesi ya Zodiak Broadcasting Station (ZBS) Tembo adadzudzula mneneri wachipanicho Jolly Kalelo pofulumira kulankhula ndi atolankhani pa za tsiku komanso malo omwe msonkhanowo udzachitikire. Kalelo adauza nyuzipepala ndi mawailesi kuti msonkhano waukulu wa MCP udzachitika pa 9 August 2013 ku Natural Resources College koma Tembo adati akuluakulu a chipanicho adangokambirana za masikuwo koma adali asadatsimikize podikira zokambirana zina ndi akuluakulu a kumalo omwe akufuna kudzachitirako msonkhanowo. ",11 "MEC Yawunika 35% ya Maboma pa Chisankho Bungwe loyendetsa chisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) likupitilira kupereka zotsatira zotsimikizika za chisankho cha president chomwe chachitika lachiwiri lapitali. Kachale: Tizingosindikiza file imodzi kuti tichite changu Malingana ndi wapampando wa bungweli Justice Dr. Chifundo Kachale, pofika 11 koloko mmawa wa lero, bungweli lakwanitsa kupereka zotsatira za maboma khumi ndi limodzi okha mwa maboma 28 a dziko lino. Mwazina Dr. Kachale ati bungweli lipitilira kupereka zotsatirazi kudzera kwa wofalitsa nkhani wake Sangwani Mwafulirwa yemwe akhale akuchita mikumano ndi atolankhani kuwadziwitsa zotsatira zomwe zatsala mpaka pamapeto powulutsa zotsatira zonse. Chinthu china chomwe chikumatenga nthawi ndi chakuti pakumabwera ma file awiri a original kuchokera kuma district, ina imapita ku parliament kuti akasunge ma record a masankho, dongosolo limenelo taliwunikira ndipo tawona kuti limatenga nthawi kwambiri chifukwa choti ma record enawo a zipani alinawo kale ndiye kwa pano tizingosindikiza file imodzi, anatero Dr. Kachale. Iwo ati mwa maboma omwe awunikidwa kale zotsatira zawo, palibe madandaulo omwe sanayankhidwe moyenera. Wapampando wa bungweli Justice Dr. Chifundo Kachale akuyembekezeka kupereka zotsatira za chisankhochi mawa. ",11 "Mpingo ndi Anthu Omwe Amasonkhana ndi Kupemphera Limodzi-Papa Papa Fransinco yemwe ndi mtsogoleri wa katolika pa dziko lonse wakumbutsa anthu kuti ngakhale kuti panopa anthu akutsatira mapemphero osiyana-siyana kudzera mu njira za makono monga makina a intaneti chifukwa cha nthenda ya Covid 19, cholinga cha mpingo ndi kuti anthu azisonkhana ndi kupemphera limodzi mmatchalichi awo. Papa Francisco wapereka chenjezo ndipo walankhula izi lachisanu pa Misa yomwe anatsogolera ku likulu la mpingo ku Vatican pamene mliri wa Coronavirus wavutitsa kwambiri zomwe zachititsa kuti anthu asiye kupita ku matchalitchi awo ndipo mmalo mwake akumatsatira mapemphero osiyanasiyana kudzera mu njira za makono zofalitsira mauthenga monga makina a intaneti ndipo iye wati akhristu akuyenera kukumbukira kuti mpingo ndi gulu la anthu omwe amabwera pamodzi ndi kupemphera powonana maso ndi maso. Nkutheka kuti pa nthawi iyi ya mliri wa Coronavirus anthu apusisika ndi kumaganiza kuti ukatha mliriwu palibenso chifukwa chomasonkhanirana malo amodzi ndi kumapemphera, anatero Papa. Iye wati zomwe zikuchitika pano ndi za kanthawi kochepa kotero kuti pambuyo pa mliri wa Coronavirus anthu adzayenera kupitiriza kusonkhana malo amodzi ndikuchita mapemphero monga zinalili mliriwu usanabwere ndipo wati anthu akuyenera kukumbukira kufunika kolandira Ambuye Yesu wokhala mu Ukaristia komanso kufunika kwa masakramenti ena monga Sakramenti la kulapa ngakhale kuti iye wati akuzindikira kuti izi ndi zovutirapo pa nthawi iyi ya mliri wa Coronavirus. ",13 " Sitilemba akunjaAnsah Pamene kalembera wachisankho walowa gawo lachisanu, mkulu wa bungwe la zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) Jane Ansah wati Amalawi asade nkhawa, chifukwa anthu a kunja salembetsa nawo mkaundula. Ansah adanena izi potsatira ndemanga za ena kuti pali chiopsezo choti nzika zina za dziko la Mozambique zikhonza kulembetsa mkaundula mboma la Mulanje. Malinga ndi anthu ena, pali chiopsezo kuti anthu ena a ku Mozambique akhonza kufuna kulembetsa nawo, makamaka ku Limbuli ndi Muloza, komwe ndi dera la mmalire ndi Mozambique. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Koma Ansah adanenetsa: Taika ndondomeko zonse kuti pasakhale wakunja woti walembetsa. Izi tikuchita poonetsetsa kuti pali mamonitala a kuderalo amenenso adzaonetsetse kuti ofuna kulembetsa ali ndi chitupa cha unzika. Mkulu wa nthambi yoona za kalembera wa unzika mboma la Mulanje, Wellingtone Kalambo wati akumanapo ndi nzika za ku Mozambique zofuna kulembetsa nawo mavoti. Taonapo mafumu a ku Muloza akupereka umboni kuti munthu ndi mMalawi, koma kuwafunsitsa, tidapeza kuti ndi a ku Mozambique, adatero Kalambo. Kalembera wa chisankho adalowa mgawo lachisanu Lolemba ndipo likuyembekezeka kudzatha pa Malinga ndi MEC, anthu 3 271 744 adalembetsa mmagawo apitawa, pomwe MEC imayembekezera kulembetsa anthu 4 619 174. Izi zikusonyeza kuti anthu 81 mwa 100 alionse amene amayenera kulembetsa ndiwo adatero. Kutsika kwa anthu amene akulembetsa kwakhudza akadaulo, a mabungwe ndi zipani zandale zina. Katswiri wa zandale wa ku Chancellor College Ernest Thindwa wati mchitidwe wamphwayi kukalembetsa ukhonza kukhala kukhumudwa kwa Amalawi ndi mchitidwe wa andale omwe amasintha mawanga akasankhidwa mmaudindo. Mwina anthu adagwa mphwayi ndi nkhani za zisankho chifukwa amakhumudwa ndi mchitidwe wa atsogoleri omwe amalonjeza zinthu zina nthawi ya kampeni koma osazikwaniritsa akasankhidwa, adatero Thindwa. Koma zipani zandale, zaalunjika ponena kuti bungwe la MEC silinafalitse bwino uthenga wa kalembera chifukwa likulimbikira pofalitsa mauthenga pa wailesi ndi nyuzipepala basi, mmalo mopitanso kumaderawo. Mneneri wa chipani cha United Democratic Front (UDF) Ken Ndanga, wati kafukufuku wawo adaonetsa kuti bungwe la MEC silidafalitse uthenga mokwanira mmadera. Tikawafunsa bwanji sanalembetse, anthu mmadera amati samadziwa zoti kalembera wafika mdera lawo. Ngati chipani, tikumapita mmaderamu kumema anthu, adatero Ndanga. Mlembi wamkulu wag ulu la United Transformation Movement (UTM) Patricia Kaliati komanso mlembi wamkulu wa Malawi Congress Party (MCP) Eissenhower Mkaka adagwirizana ndi Ndanga podzudzula MEC. Ndikunena pano ndili ku Mulanje kumene kalembera ali mkati koma sindinaone galimoto ya MEc ngakhale chimkuzamawu kumema anthu kukalembetsa. Mkaka adati chipani chawo, chomwe chakhala chikupempha MEC kuti ibwereze kalembera mmadera ena, chimayembekezera kuti pofika gawo lachinayi la kalembera, zinthu zikhala zitasintha koma mmalo mwake zikunkira kuonongeka. Mgawo loyamba ndi lachiwiri, zidali zomveka kuti uthenga udali usadamwazidwe mokwanira koma mgawo lachinayi tizikamba nkhani imeneyi? Ayi sizoona MEC ikadawonapo bwino, adatero Mkaka. Mkulu wa mgwirizano wa mabungwe okhudzidwa ndi zisankho la Malawi Electoral Support Network (Mesn) Steve Duwa adagwirizana ndi zipanizi kuti MEC yalephera kumwaza mauthenga a kalembera. Ndidali ku Thyolo ndi Luchenza komwe anthu samaonetsa chidwi ndipo ntafunsa, makhansala ngakhaleso anthu amati sadalandire uthenga uliwonse woti kukuchitika kalembera mdera lawo kutanthauza kuti ntchito ikadalipo, adatero Duwa. Koma malinga ndi Ansah, palibe kuwiringula kulikonse koti mauthenga sadamwazidwe chifukwa MEC ndi mabungwe ena monga National Initiative for Civic Education (Nice) Trust ayesetsa kumwaza mauthenga. Kupatula njira yomwaza mauthenga pa wailesi, timagwiritsanso ntchito galimoto zokhala ndi zimkuzamawu. Mgawo loyamba, tidagwiritsa ntchito galimoto 15, gawo lachiwiri galimoto 14, gawo lachitatu galimoto 18 ndipo gawo lachinayi galimoto 17, adatero Ansah. Iye adati bungweli lidzaunika pamapeto pa zonse ngati nkoyenera kubwereza ntchito ya kalembera mmaboma omwe sizidayende bwino. ",11 " Tidasala masiku 52 kuti Mulungu atiunikire Nthawi zambiri, anthu timatenga banja ngati sitepe pamoyo wathu basi koma tikalingalira momwe banja la mbusa komanso mlembi wa mkulu wa mpingo wa CCAP Reverend Vasco Kachipapa Banda ndi mkazi wake Madalitso Nyoli, mibadwo yobwerayi idzazindikira momwe banja la umulungu limakhalira. Awiriwa akuti adakumana mu 1992 onse atasankhidwa kupita kusukulu ya sekondale ya Mitundu ndipo chikondi chawo chidayamba mu 1994 koma uku sikudali kuyamba kwa banja poti zambiri zidadutsapo. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Rev. Kachipapa adati mizati itatu ndiyo idagwira ntchito kuti awiriwa atseguke mmaso kutidi adalengedwa kudzakhala limodzi ndi kutumikira Chauta ngati bambo ndi mayi komanso odyetsa ndikusamala nkhosa zake. Kachipapa ndi Madalitso: Lero ndi banja Mzati woyamba, ineyo ndidadwala tikadali kusukulu mpaka ndidapita kunyumba. Nditapeza bwino nkubwerako, Madalitso adabwera kudzandizonda ndipo aka sikadali komaliza. Pamenepa ndidazindikira kuti ndi umunthu weniweni, adatero Kachipapa. Iye adati chikondichi sichidasanduke mapeto azonse ayi koma chiyambi cha kudzifunsa ndi kupempha utsogoleri wa Mulungu. Mchaka cha 1997, tonse awiri tidayamba mapemphero ndi kusala kwa masiku 52 (Loweruka lokhalokha) kupempha Mulungu kuti atiunikire ngatidi tidali oyenera kukwatirana. Ndi mzati wachiwiri ndipo mzati wachitatu udali nthawi yomwe ine ndimapanga maphunziro a zaubusa ku Zomba, mkazi wanga adali atayamba kale ntchito ndipo adandithandiza kupereka malowolo ake omwe, adatero Kachipapa. Iye adati Chauta atavomereza zonse, ndondomeko zoyenera zidatsatidwa kufikira nthawi ya chinkhoswe mchaka cha 1998 ndipo kenako ukwati woyera ku Ntchisi CCAP. Ndimakonda mkazi wanga kwambiri chifukwa cha mtima wake wabwino, amakonda kupemphera kwambiri ndipo simkazi wanga chabe koma mzanga muuzimu, adatero Kachipapa. Nawo mayi a kunyumba akuti (Madalitso) akuti abusawa ndi bambo wabwino wokonda banja lawo ndi wodziwa kusamala. Ndi bambo abwino kwambiri odziwa udindo wawo ndiokonda banja lawo komanso kusamala ana awo. Timapemphera limodzi, kuyenda limodzi, kudya limodzi mwachidule timapangira zinthu limodzi, adatero mayiwo. ",13 " Afa atamwa bibida wosadyera Mneneri wa polisi ya Nkhotakota Williams Kaponda watsimikiza kuti bambo wina kumeneko wakabzala chinangwa atapapira mowa osadyera. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kaponda adati malinga ndi achibale, Damson Wasiya, 34, malemuwo omwe ndi Francis Phiri adapita kukapopa mowawo Lamulungu pa 8 November mbomalo. Achibalewo auza apolisi kuti malemuwa adapezeka usiku akuchokera kopopa mowawo ali lamba! Mumsewu, zomwe zidakhudza ofuka kwabwino amene adamutengera kunyumba. Ataona kuti mbaleyo akuoneka moti samapeza bwino, adathamangira naye kuchipatala cha boma komwe madotolo adakatsimikiza kuti adali atafa, adatero Kaponda yemwe adati zotsatira za achipatala zidaonetsa kuti malemuwo adafa chifukwa chomwa wosadyera. ",15 " Zitupa zaunzika zina zasowa Zitupa 93 893 za uzika mboma la Kasungu zasowa. Tamvani itha kuvumbulutsa. Izitu zadziwika pamene bungwe lolembera unzika la National Registration Bureau (NRB) layamba kupereka zitupazi kwa eni. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mneneri wa wa bungwe la NRB Norman Fulatira watsimikiza izi ndipo wati: Ili si vuto lalikulu mtima ukhale mmalo. Maboma amene adayambirira kulembetsa za unzika a Mchinji, Dowa, Kasungu, Salima, Nkhotakota ndi Ntchisi ayamba kulandira ziphaso zawo zomwe zaonetsa kuti nkhope zina zikusowa. Anthu 93 893 amene amayembekezera kulandira zitupazi adadzidzimuka kuona kuti maina awo palibe pamene anzawo nkhope zawo zatuluka ndipo alandira zitupa. Anthu amene dzina lawo lasowa mbomalo ati chiyembekezo chawathawa ngati angalandire zitupa zawo. Lufeyo Mwanza wa mbomalo adauza Tamvani kuti chikhulupiriro pa NRB achotsa kuti zitupa zawo zidzapezeka. Inde akutilimbitsa mtima kuti zitupa zathu zibwera komabe chilimbikitso chimenechi nchosakwanira. Tikuganiza kuti zasowa ndipo mwayi wokhala ndi zitupazi watiphonya, adatero Mwanza. Iye adati pakhota nyani mchira nkuti anzawo amene adajambulitsira limodzi zitupa zawo zatuluka koma iwo zavuta. Komabe Fulatira akuti mwa maina 1.7 miliyoni omwe adalembedwa moyambirira, mayina 1.5 miliyoni okha ndiwo adatumizidwa kuti akatulutse zitupa ndipo maina enawo amaunikidwa ngatidi ali a Malawi. Anthu [asathamange magazi] kuti zitupa zawo zasowa, chifukwa tikukonza ndipo alandira zonse zikatheka bwinobwino, adatero Fulatira. Iye adatinso zitupa 200 000 za mndime yoyamba ya kalemberayu ndizo sizidakonzedwe ndipo anthu omwe zitupa zawo zasowawo akhoza kukhala mgululi. Pologalamuyi ndi ya a Malawi choncho timayenera kuunika maina bwinobwino kuti tisapezeke zoti tikupeleka ziphaso kwa alendo. Zonse zikatheka, aliyense yemwe ndi nzika ya dziko lino ndipo adalembetsa, adzalandira chiphaso, adatero Fulatira. Senior Chief Kaomba ya mboma la Kasungu idati iyo siyikuonapo vuto pa nkhaniyi chifukwa zitupa zomwe zikusowa nzochepa poyerekeza ndi zomwe zapezeka. Aka nkoyamba boma kupanga kalembera ngati uyu ndiye pa mayina 1.5 miliyoni, kusowa maina okhawo si chodandaulitsa kwenikweni ndipo tikuyenera kumvetsetsa, adatero Kaomba. Iye adapempha anthu kuti adekhe chifukwa NRB ikulongosola. Boma lidakhazikitsa ntchito ya kalembera wa unzika kuti lizitha kuzindikira anthu ake makamaka powathandiza pa ntchito zofunika ngati za umoyo, maphunziro komanso kuwapeza mosavuta akasowa kapena kutsakamira mmaiko a eni. Kalembera yemwe ali mkati pano adayamba pa 24 May chaka chino ndipo akuyembekezeka kutha mu December. Malinga ndi Fulatira, ntchitoyi idzakhala ikupitilira mpaka kalekale. Iyi idali ndime yokhazikitsira ndipo aliyense amayenera kulembetsa mmalo omwe tikuchita kukhazikitsa koma kuyambira January chaka chamawa, omwe sadalembetse, aziloledwa kukalembetsa mmaofesi athu a mmaboma kapena kotumizira makalata [post office] yomwe angayandikane nayo, adatero Fulatira. Iye adatinso amene ayambe kulembetsa chaka chamawa koyamba azidzalembetsa ulere pamene kwa omwe adasowetsa chitupa ndipo akufuna china, azidzapemphedwa kupereka kangachepe. Kwa amene amakhala kutali ndi post office sadzavutikanso chifukwa NRB idzidzayendera mmadera kuthandiza Amalawi malinga ndi Fulatira. ",11 "Akhristu Alumikizana Pothandiza Atumiki Bungwe la akhristu eni ake mu arkidayosizi ya Blantyre lati likufuna kulimbikitsa ntchito zotukula arkidayosizi-yi komanso kusamalira atumiki amu mpingo-wu. Wapampando wa akhristu mu arkidayosizi-yi a Joseph Kachala ayankhula izi pomaliza pa msonkhano omwe anali nawo Loweruka pa 29 February ku Limbe Cathedral Mu mzinda Wa Blantyre. Iwo anati ntchito yawo ndi kuwonetsetsa kuti akhristu akudziwa udindo wawo pothandiza mpingo komanso atumiki mu mpingowu monga asisitere, ansembe, abulazala ndi ena ambiri. Timakambirana kuti ngati akhristu tikuyenera kuwonetsetsa kuti atumiki mu mpingowu akusamalidwa moyenera mmoyo wawo wa thupi kuti azititumikira mopanda chowabwezeretsa mmbuyo, anatero a Kachala. ",13 " Zipani za moyo zionekeCMD Kodi zipani zinazi zili moyo? Nthawi yofukula yakwana mzipani pamene bungwe loona mgwirizano wa zipani zosiyanasiyana la Centre for Multiparty Democracy (CMD) lalengeza zokumana ndi akuluakulu a zipani. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Bungweli laitana zipani 41 zomwe zidalembetsedwa koma zilibe aphungu mNyumba ya Malamulo. CMD ikuchita izi kutsatira kudutsa kwa bilo yokamba za kayendetsedwe ka zipani imene mwa zina ikuti zipani zimene sizikuoneka zichotsedwe mkaundula pakatha miyezi 12. Tenthani: Tiwaimbira Kalata yomwe CMD yatulutsa ikuti eni zipanizo atumize ku bungwelo maina a mtsogoleri wawo ndi mlembiatumizenso nambala, madera amene akukhala. Mkulu wa bungwelo, Kizito Tenthani adati zipanizo zikatumiza maina ndi manambalawo adzawaimbira kuti akumane nawo kuti awafotokozere zomwe zili mbiloyo. Iye adati: Ngati satiyankha mwina zisonyeza kuti kulibe munthu. Pakatha miyezi 12 ndiye kuti zisonyeza kuti chipanicho chazimirirakusonyeza kuti osindikiza zipani atha kuchifufuta. Mwa zipani zomwe zaitanidwa ndi cha The Malawi Democratic (MDP) chomwe mwa ena amene adachiyambitsa ndi Kamlepo Kalua yemwe lero ali ku PP. Chipani china ndi cha Malavi Peoples Party (MPP) chomwe adayambitsa ndi Uladi Mussa amene akungoyendayenda. Adali ku UDF asadasinthe golo kupita ku DPP. Madzi atachitako katondo adalumphamo kugwera mu PP, lero wasinthanso golo kubwerera ku DPP. Titamuimbira foni ngati alembere bungweli monga iye mtsogoleri, Mussa adayankha modabwa. Malavi ndiye chiyani? adafunsa. Aaa! Nanga ine mesa ndidachokako, ndidali ku PP pano ndili ku DPP. Inuyo mungopitako mukaone atsogoleri amene apitawo osati muzindifunsa ine, adatero. Koma Tenthani ali ndi chikhulupiriro kuti zipanizi ziwalembera. Ine ndi mkulu wa CMD, nditachoka lero sizikutanthauza kuti CMD yatha, atsogoleri otsalawo ndiwo angayankhepo ngati atafunidwa. Titsimikiza kuti mzipanizo mudatsala ena amene atilembere, adatero. Mndandanda wa zipanizi ndi womwe udalembetsedwa mdziko muno kuti ndi zipani zokhazikika. Zina mwa zipani zoitanidwazo zidamveka pachisankho cha 1994 osamvekanso. Izi ndi monga cha Congress for the Second Republic cha Kanyama Chiume, Malawi Democratic Union cha Amunandife Mkumba, United Front for Multiparty Democracy, Malawi National Democratic Party ndi zina zotero. Dziko lino lili ndi zipani zoposera 50. ",11 " Wofuna kugulitsa alubino achimina Bwalo la milandu la Mzuzu majisitireti lalamula Philip Ngulube, wa zaka 21, kuti akakhale kundende ndi kukagwira ntchito yakalavulagaga kwa zaka 6 atamupeza ndi mlandu wofuna kuba msungwana wachialubino ndi cholinga chofuna kumupha. Ngulube, yemwe adali mphunzitsi wodzipereka pasukulu yapulaimale ya Mongo mboma la Mzimba, adagwirizana zomanga banja ndi msungwanayo, wa zaka 17, yemwe ankaphunzira pasekondale ya Mzimba. Escom in free-for-all fuel scam Wait gets longer Secrecy over party funders Ngulube (akukokera kabudulayo) kutuluka mkhoti ulendo wa kundende Koma mphuno salota, Ngulube adali ndi maganizo ogulitsa msungwanayo kwa munthu wajohn chirwa malonda yemwe ndi mbadwa ya mdziko la Tanzania. Koma msungwnayo adapulumukira mkamwa mwa mbuzi mbadwa ya ku Tanzaniayo itakatsina khutu apolisi za malonda omwe Ngulube adali nawo. Apolisi ndi luntha lawo, adapita kwa Ngulube ngati ofuna kugula mualubinoyo. Apa mpamene Ngulube adakwidzingidwa ndi unyolo zitapezekadi kuti amagulitsa mtsikana wachikondi wakeyu pamtengo wa K6 miliyoni. Nkhani idapita kubwalo la majisitireti Gladys Gondwe komwe adazengedwa mlandu wofuna kuba munthu ndi cholinga chofuna kumupha, womwe adaukana. Koma Lolemba lapitali, Gondwe muchigamulo chake chomwe chidatenga mphindi zisanu zokha, adalamula kuti Ngulube akagwire gadi kwa zaka zisanu ndi chimodzi. Gondwe adati mlandu womwe amazengedwa Ngulube uli ndi chilango cha zaka zisanu ndi ziwiri. Iye adati adaganiza zopereka zaka 6 ndi cholinga chakuti Ngulube adziwe kuipa kwa mchitidwe wofuna kuba munthu. Woweruzayu adati nzomvetsa chisoni kuti msungwanayo adasiya sukulu chifukwa cha kusowa mtendere ndi zomwe adachita Ngulube. Iye adati izi nzotsutsana ndi malingaliro a mabungwe ndi boma polimbikitsa maphunziro a asungwana. Wozenga mlandu wamkulu kuchigawo cha kumpoto, Christopher Katani, adati ndi wokondwera ndi chigamulo chomwe bwalo la milanduli lidapereka. Iye adati zaka 6 ndi zokwana potengera kuti mlandu womwe amazengedwawo umayembekezereka kulandira chilango cha zaka 7. Katani adatinso ndi wokhurira poti nkoyamba kumpoto bwalo lamilandu kutumiza munthu kugadi chifukwa cha mchitidwe wakuba anthu achialubino. Ngulube polandira chilangochi, adaoneka kuti adali woyembekezera matherowo chifukwa sadaoneke kudodoma kulikonse. ",7 "Ndi Udindo wa Amalawi Kutetedza Chilengedwe- SVP Bungwe la zachifundo mu mpingo wa katolika la St. Vincent De Paul (SSVP) lati kusintha kwa nyengo kwakhala gwero lalikulu la mavuto ambiri amene anthu mdziko muno akukumana nawo kuphatikiza kusowa kwa malo okhala abwino komanso chakudya. Bungwe la SVP kupereka zofunda kwa ovutika Bungweli lanena izi lamungu pa 22 February 2020 ku likulu lake mdziko muno mu mzinda wa Blantyre pothilira ndemanga pa mapurojeketi omwe bungweli lili nawo mchaka chino. Mkulu wa bungweli mdziko mu a Charles Kimu anati anthu ambiri omwe bungweli lawafikila mbuyomu ndi anthu amene anakhuzidwa ndi kusintha kwa nyengo monga kusefukila kwa madzi komanso chilala, choncho vutoli ndi lalikulu pakati pa mzika za dziko lino. Tapelera katundu osiyanasiyana kwa mawanja amene anakhuzidwa ndi madzi otsefukila komanso kwa anthu okhuzidwa ndi ngamba ochuluka ntchaka cha 2019 choncho vutoli likuvutitsa miyoyo ya anthu ambiri dziko muno, anatero a Kimu. A Kimu anati kupatatula kuwapasa zinthu zokhazikika anthu amene anakhuzidwa ndi kusintha kwa nyengo komanso osowa, ndi kofunika kwambiri kuti dziko lino liyike chidwi chake posamalira chilengedwe pozindikira kuti chilengedwe ndi gwero la zofunika zambiri pa umoyo wa munthu. A Kimu kupereka zovala kwa ovutika Iwo anati chaka cha 2020 Bungweli lilindimalingaliro okonzera nyumba za anthu omwe anakhuzidwa ndi mvula yamphavu mchaka cha 2019 ndipo ndondomekoyi iyambila mu akidayosizi ya Blantyre. Anthu amene anakhuzidwa ndi mvula ya mphavu chaka chatha akukhalabe mnyumba zamavuto monga zamingalu choncho ndikofunika kuti kuwafikila anthuwa, anaonjezera motero a Kimu. Mwazina bungweli mchaka cha 2020 liphunzitsanso ntchito zamanja mwaulele anthu ochokera ku mabanja ovutikikitsitsa ngati mbali imodzi yowalimbikitsa anthuwa kuimba paokha pa chuma. Bungwe la SVP kupereka chimanga kwa anthu osowa Wapampando wabungweliyu anapitiliza kupempha anthu amene amalandira thandizo losiyanasiya kuchokela kwa akufuna kwabwino kuti azisamala thandizolo chifukwa kutelo zimaonetsa mtima othokoza. Zimamvetsa chisoni kuona anthu akugulitsa katundu yemwe alandira kwa akufuna kwa bwino, anadandaula choncho a Kimu. Bungwe la St. Vincent de Paul liyamba mdziko muno ku Zomba dayosizi pa 17 Okotobala, mchaka 1970 ndi bambo Berck a mdziko la France. ",18 " Kutentha koonjeza kuzinga maiko A nthambi yoona za nyengo mdziko muno auza Amalawi kuti alimbe mtima chifukwa nyengo yotentha yomwe yakhala mdziko muno kwa sabata ziwiri zapitazi, kupitirira kwa sabata zikubwerazi. Kuchokera sabata yatha, dziko lino lakhala likutentha ngati nganjo ya moto moti madera a kunsi kwa chigwa cha mtsinje wa Shire kutenthaku kumafika pa 450C pomwe madera ena kumafika pa 350C. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Anthu akhala akudandaula kuti kutenthaku kukusowetsa mtendere. Zikuoneka kuti nyengo yotenthayi yatikakamira chifukwa a nthambi yoona zanyengo adalengeza Lolemba kuti Amalawi angovala zilimbe chifukwa nyengoyi ipitirira kwa sabata zikubwerazi. Komatu si dziko lino lokha lomwe lakhaula ndi kutenthaku chifukwa maiko ena ambiri a mdera la kummwera mu Africa la Southern African Development Community (Sadc) monga Botswana, Eswathini, Mozambique ndi ena. Malinga ndi kalata yomwe idatulutsa nthambi yoona za nyengo mbungwe la Sadc Lolemba pa October 28, yachenjeza anthu kuti kutentha molapitsa mmaiko a mderali. Pomwe kalata yochokera ku nthambi yoona za nyengo mdziko muno ya Climate Change and Meteorological Services yomwe adatulutsa ndi mkulu wa nthambiyo Jolamu Nkhokwe idalongosola kuti kuchokera Lamulungu pa October 27 kufika pa November 3, kutentha ndi dzuwa kupitirira. Kalatayo yati sabata yapitayi madera monga Lengwe National Park mboma la Chikwawa kudatentha 45C pomwe ku Mwanza ndi Nsanje kudafika 44C. Koma kuchokera Lachitatu pa November 30, mitambo iyamba kumangana mmadera ena a dziko lino zomwe zikhonza kubweretsa mvula ya mphepo ya mkuntho komanso ziphaliwali, ikutero kalatayi. Malinga ndi Nkhokwe aka si koyamba kuti mdziko muno mutenthe chonchi maka mmadera a kunsi kwa chigwa cha mtsinje wa Shire koma kuti chaka chino ndi dziko lonse lomwe latentha. Nkhokwe adati ana ndi anthu achikulire ngofunika chisamaliro kwambiri pa nthawiyi. Katswiri pa nkhani za sayansi, chilengedwe yemwenso amadziwa bwino za kusintha kwa nyengo, Professor Sosten Chiotha adati kutenthaku ndi zina mwa zizindikiro za kusintha kwa nyengo. Timadziwa kuti timakhala ndi nyengo zosiyana nthawi ndi nthawi ndipo ndi mmene zikuyenera kukhalira, koma kusinthaku kukakhala kowonjeza kuposa mmene zikuyenera kukhalira, zimalowa mgulu la kusintha kwa nyengo, adalongosola Chiotha. Koma iye adalongosolanso mwachindunji kuti nyengo ikangosintha kamodzi sikusintha kwa nyengo koma kusinthaku kumayenera kukhale kwa nthawi yaitali. Malinga ndi Chiotha, malipoti a zanyengo mdziko muno akuonetsa kuti kusinthaku kwakhala kukuchitika kwa nthawi yaitali ndithu. Naye bwanamkubwa wa mboma la Karonga, Frank Kalilombe adati bomalinso kwakhala kukutentha molapitsa kuchokera sabata yapitayi. Iye adati mpofunika kupeza njira zoti ana ndi achikulire adziwe zoyenera kuchita panthawiyi poopa ngozi zodza mwadzidzidzi monga kukomoka ndi zina kaamba ka kutenthaku. ",18 "Episkopi Apempha Amayi Adzipereke Pofalitsa Mthenga Wabwino Episcope wa dayosizi ya Chikwawa Ambuye Peter Musikuwa apempha amayi akatolika mdziko muno kuti akhale odzipereka pa ntchito yofalitsa uthenga wabwino ku matchalitchi amene amayiwa akupezekako. Ambuye Musikuwa omwenso ndi mkulu woona zachipembezo ku likulu la mpingo wa katolika mdziko muno amalankhula lamulungu pambuyo pamwambo wa misa yotsekera msonkhano wa amayi mdziko muno womwe umachitikira ku sukulu ya ukachenjede ya DMI mu dayosizi ya Mangochi. Umodzi mwa misonkhano ya bungwe la amayi Iwo ati mpingo ukuyembekeza kusitha kwakukulu kuchokera kwa amayiwa pambuyo pa msonkhanowu monga pankhani zosamalira zachilengedwe, zaumoyo komanso kukonda ndi kulimbikitsana kuwerenga bukhu loyera. Tikuyembekezera kuti zinthu zikasintha ku maparishi komwe amayiwa akuchokera. Tikukhulupilira kuti tiwona kusintha pa nkhani ya zokhudza kusamalira chilengedwe ndi zina zambiri, anatero Ambuye Musikuwa. Polankhulapo wachiwiri kwa wapampando wa bungwe la amayi mdziko muno mayi Magdalene Masamba Nkhope apempha amayi omwe anafika ku msonkhanowu kuti akagawane ndi anzawo mmadayosizi awo mfundo zomwe atenga ku msonkhanowu. Msonkhanowu omwe unali wa masiku asanu unayamba lachitatu pa 11 mpaka lamulungu pa 15 December 2019 ndipo wachitika pamutu wakuti Amayi akatolika tayitanidwa kukhala oyera mtima kuti tiyeretse dziko lapansi kwathunthu. ",13 "Bwanamkubwa Wapempha Mabungwe Athandize Khonsolo Polimbana Ndi Coronavirus Bwanamkubwa wa boma la Zomba Dr. Raphael Piringu wapempha mabungwe omwe akugwira ntchito zawo mboma la Zomba kuti athandidze ndi zipangizo zosiyanasiyana zothandiza anthu kuti asatenge kachirombo ka Coronavirus. Piringu: Anthu owona odwala mchipatala akuchuluka Dr. Piringu amayankhula idzi lachitatu ku Zomba pomwe amakumana ndi akulu akulu a mabungwe komanso oyimililira zipembedzo (Pastors Fraternal). Iwo apemphanso mabungwewa kuti apereke uthenga mzipatala kuti anthu owona odwala asamachuluke. Dr Piringu ati misika yambiri ya mbomalo ilibe mipanda choncho apemphanso mabungwewa kuti aphunzitse anthu nkhani yosamba mmanja. Mmau ake wapampando wa mabungwe omwe si a boma mboma la Zomba a Newton Sindo apempha mabungwewa kuti akamapereka zinthu kwa anthu mmadera akumidzi ndibwino kuti adziwaphunzitsa kagwiritsidwe ntchito kazinthu zomwe aperekazo. ",6 "Aphungu ku Uganda Akufuna Mkazi wa Mtsogoleri wa Dzikolo Akonze Maphunziro Nyumba ya malamulo mdziko la Uganda yati ikufuna mkazi wa mtsogoleri wa dzikolo, Janet Museveni afotokoze bwino pa nkhani ya kusayenda bwino kwa maphunziro mdzikolo. Malipoti a wailesi ya BBC ati speaker wa nyumbayi Rebecca Kadaga analembera kalata Museveni yemwe ndi nduna yowona za maphunziro kuti akawonekere mnyumba ya malamuloyi lachiwiri ndi kukafotokoza bwino chomwe chikuchititsa kuti dongosolo latsopano la maphunziro lisayende bwino. Museveni akuti sanapite ku nyumbayi ndipo wati apitako lachinayi likudzali. Aphungu a nyumba ya malamulo mdziko la Uganda akudzudzula unduna wa za maphunziro poyambitsa dongosolo latsopano la maphunziro mdzikomo ngakhale nyumba ya malamulo inalamula kuti dongosololi liyimitsidwe kaye ponena kuti ndi lolowetsa pansi maphunziro. Aphunguwa akuti ndi okudzidwanso kwambiri kaamba ka kusowa kwa mabukhu komanso kusaphunzitsidwa bwino kwa aphunzitsi pa dongosolo latsopanoli. ",3 " Khama Khwiliro: Katakwe pa nyimbo zauzimu Khama Khwiliro ndi mmodzi mwa oimba nyimbo zauzimu amene ambiri otsata nyimbozi amamudziwa. CHIMWEMWE SEFASI adakumana naye ndipo adacheza motere: Ndikudziwe Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Dzina langa ndine Khama Khwiliro, ndidabadwa pa 15 April 1983. Kwathu ndi mmudzi mwa Mtengula, kwa T/A Chikowi ku Zomba. Kodi udakwatira? Maso patsogolo: Khwiliro Khama ali pabanja ndipo adakwatira Jackina Meleka ndipo adadalitsidwa ndi mwana mmodzi, dzina lake Tawina. Kodi zoimbaimba udayamba liti? Ndidayamba kuimba mma 1990. Koma mu 2010 mpamene ndidatulutsa chimbale changa choyamba chomwe mutu wake ndi Nthawi Yanga Yakwana. Kodi uli ndi zimbale zingati? Inetu ndili ndi zimbale ziwiri: Nthawi Yanga Yakwana komanso Ndaona Kuwala. Uthenga wako wagona pati nanga umaimba zamba zanji? Uthenga wagona pa za mawu a Mulungu okamba zoyenera kuchita monga Akhristu makamaka nthawi yotsiriza ino. Nyimbo zikulukidwa mu zamba monga manganje, kwaito ndi zamba zina za kwathu kuno. Pambali poimba umagwiranso ntchito ina? Nanga umakonda chiyani ngati sukuimba? Inetu ndimagwira ntchito ku Blantyre Synod Health and Development Commission komanso ndikakhala kuti ndili ndi mpata, ndimakonda kucheza ndi anthu osiyanasiyana. Kumbali ya zakudya, ndimakonda nsima ya chisoso ndi chambo. Kuimba umafuna utafika nako pati? Ndimafuna kuimba kutafika ngati mmene anzathu akunja amachitira komanso anthu azitha kukwanitsa kusamala mabanja awo kudzera mkuimba ndi kupeka nyimbo. ",13 "Muyambitsi Wa Radio Maria Pa Dziko Lonse, Wamwalira Yemwe anayambitsa wailesi za Radio Maria pa dziko lonse a Emmanuel Ferrario amwalira ali ndi zaka 90 zakubadwa. A Ferrario amwalira masana wa pa 08 July 2020 mdziko la Italy ndipo pa nthawi ya imfa yawo, anali ali president opuma wa World Family of Radio Maria. Muyambitsi wa Radio Maria pa dziko lonse-Ferrario Dongosolo lokhudza maliro ndi Nsembe ya Misa yotsanzikana ndi malemu President Emmanuele Ferrario lilengezedwabe. Radio Maria Malawi idzawakumbukira malemu President Emmanuele Ferrario ngati tate amene amakonda ndi kufunitsitsa kuti Radio Maria Malawi ikule ndi kufikira madera ambiri a kuno Malawi. President Ferrario pamodzi ndi anthu ena anayambitsa Radio Maria ngati ka wayilesi kakangono ka Parish ya Erba mdziko la Italy mchaka cha 1982. President Ferrario adali munthu mmodzi yemwe amakonda Amayi Maria koposa ndipo chidwi chake chofuna kutsekula wailesiyi chinayamba pomwe anachita malonjezo kwa Amai Maria pa matenda a mkazi wake kuti ngati adzachiritsidwa ku nthenda ya cancer, iye adzagwira ntchito mosalekeza yofalitsa mthenga wabwino wa Amayi Maria. Mkazi wake atachiritsidwa iye adagulitsa imodzi mwa kampani zake, ndalama zake nayendetsera wayilesi imene imafalitsa za Amai Maria a ku Medjugorje imene inakhazikitsidwa mchaka cha 1983. Pambuyo pa imfa ya mkazi wake mchaka cha 1984, President Ferrario anapitiriza kuthandiza komanso kutumikira ku wayilesiyi yomwe idali ya Parish. Pambuyo pake adagulitsa kampani yake ina yopanga zakudya zochokera ku mkaka ndi kuyika chuma chake chonse mu ntchito zokulitsa ka wayilesi kameneka. Mchaka cha 1986 ndi pamene adakhazikika mu ntchito zoyendetsa wayilesi ndipo mchaka chotsatira iye adasankhidwa kukhala President wa wayilesi imeneyi. Mchaka cha 1987 adakumana ndi bambo Livio Fanzaga, wansembe wina yemwenso adali wokonda wayilesi-yi ndipo limodzi adagwirizana mfundo zikulu zikulu ziwiri zoyendetsera wayilesi yi imene idali itayamba kukula. Mfundo yoyamba inali kukana kuchita malonda amtundu wina uliwonse pa wayilesiyi ndipo mfundo yachiwiri inali kukonza dongosolo la mapologalamu omwe tsinde lake lagona pa mapemphero, Katekisimu komanso Misa. Ichi ndiye chidali chiyambi cha mulakuli wa mphamvu wotchedwa Radio Maria umene unakula kuchoka pa wayilesi ya pa Parish kufika pa wayilesi ya yomveka mdziko lonse la Italy. Kudzera mu uneneri wa Amai Maria wailesiyi yakwanitsa kufikira mmaiko 80 pa dziko lonse lapansi ndipo ikuyembezeka kupita patsogolo maka kufikira maiko a ku Middle East ndi ena ambiri. Mzimu wa President Emmanuel Ferrario uwuse mu mtendere wosatha. ",14 "Mulungu Amasankha Munthu Ndi Cholinga-Papa Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco, wati Mulungu amasankha munthu ndi cholinga. Malinga ndi malipoti a Vatican Radio, Papa walankhula izi lachitatu ku likulu la mpingo ku Vatican. Iye wati Mulungu anasankha Davide kukhala mfumu ngakhale kuti pa nthawiyi Davide anali wachichipere popeza Mulungu anali naye cholinga. Papa Francisco wafotokoza kuti Davide anali mbusa wa ziweto ku tchire koma Mulungu anamusankha kuti asiye kusamalira ziweto ndipo kuti mmalo mwake akhale mbusa wa anthu. Iye wati zimene Mulungu amaona mwa munthu pompatsa udindo ndi zosiyana ndi zomwe anthu angaone ndi maso awo. Iye wati Davide anali ndi zofooka zake ngati munthu komabe Mulungu anamusankha kukhala mfumu. Papa Francisco wati chinthu chochititsa chidwi ndi chakuti ngakhale Davide anali ndi zofooka zake iye anali kukonda kupemphera. Ndipo Chifukwa chokonda kupemphera nthawi iliyonse akachimwa Davide anali kulapa machimo ake kuti Mulungu amukhululukire. Pamenepa iye watsindika za kufunika kwa mapemphero mmoyo wa munthu aliyense. Papa Francisco wati munthu amene amakonda kupemphera amatsogoleredwa mmoyo wake ndi Mulungu. ",13 " Lamulo la chuma cha pulezidenti liunikidwenso Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mmodzi mwa akatswiri a za malamulo Edge Kanyongolo wati lamulo lomwe likukamba za katundu ndi chuma cha atsogoleri a dziko liunikidwenso ndi cholinga chopatsa mphamvu zochuluka kwa Amalawi akafuna kufufuza atsogoleri omwe akugwiritsa ntchito maudindo awo podzikundikira chuma. Izi zadza pamene dziko la Malawi ladzidzimuka ndi kuchuluka kwa chuma cha mtsogoleri wakale wa dziko lino malemu Bingu wa Mutharika ngakhale kuti adakhala pampandowu kwa kanthawi kochepa. Kwa zaka 8 zokha zimene Mutharika adakhala pulezidenti wa dziko lino, chuma chake chidawonjezekera modabwitsa kuchoka pa K150 miliyoni panthawi imene asankidwa kukhaka pulezidenti kufika pa K61 biliyoni mmene ankamwalira, zomwe Amalawi ambiri akuti zachulukitsa poyerekeza malipiro amene mtsogoleri wa dziko amalandira pamwezi. Malamulo a dziko lino amafotokoza kuti Pulezidenti ndi wachiwiri wake sakuyenera kudulidwa msonkho pamalipiro awo apamwezi. Kuphatikiza apo, ndi misonkho ya anthu osauka, atsogoleriwa amakhala ndi bajeti yogulira chakudya komanso ziwiya za mnyumba zawo. Pakatha zaka zisanu zilizonse, atsogoleriwa alinso ndi ufulu woitanitsa kuchokera kunja galimoto imodzi ya kumtima kwawo popanda kupereka msonkho wotchedwa Duty ku bungwe lotolera msonkho la Malawi Revenue Authotiry (MRA). Kwa nthawi yaitali, atsogoleri ena akhala akugwiritsa ntchito mphamvu ndi ufulu umene lamulo limawapatsa poitanitsa katundu wochitira bizinesi zosiyanasiyana koma osapereka msonkho ku MRA, zomwe zikutsutsana ndi malamulo a dziko lino. Pofuna kuthana ndi mchitidwewu, boma lidakhazikitsa bungwe lapadera la Special Law Commission (SLC) mchaka cha 2006 ndi cholinga choti liunikenso bwino gawo 88 la malamulo a dziko lino. Ntchito yake yaikulu inali kukonza lamulo lokakamiza Pulezidenti, nduna komanso akuluakulu ena ogwira ntchito mboma kunena poyera mmene chuma chawo chilili asanalumbiritsidwe pamaudindo osiyanasiyana. Kafukufuku wa bungweli adasonyeza kuti kupatula lamulo lokakamiza atsogoleri kubwera poyera pakatundu yemwe ali nawo, maiko monga Uganda, Kenya ndi Tanzania adaikanso ndondomeko ndi mfundo zowonjezera zothandiza munthu akafuna kudziwa kapena kutsatira momwe chuma cha atsogoleri awo chikuchulukira kudzera mumaudindo awo ngati pulezidenti, nduna kapena phungu wa Nyumba ya Malamulo. Mwa mfundo zina, bungweli lidavomereza kuti munthu wogwira ntchito mboma sakuyenera kugwiritsa ntchito udindo wake podzikundikira yekha chuma kapena anzake; asagwirenso ntchito zina kupatula yomwe adalembedwa ndi boma; apewe kugwira ntchito zomwe sizikugwirizana ndi udindo wake komanso asagwiritse ntchito udindo wake kapena katundu wa boma molakwika. Ngakhale izi zili choncho, zikuwoneka ngati Amalawi alibe mphamvu komanso lamulo lomwe lingawaikire kumbuyo akafuna kulondoloza chuma cha atsogoleri awo. Izi zikupereka mwayi kwa atsogoleriwa kugwiritsa ntchito maudindo awo momwe angafunire popanda wina kuwafunsa. Kanyongolo adati izi zikusonyeza kufooka kwa malamulo a dziko lino nchifukwa chake atsogoleri akutengerapo mwayi. Iye adati lamulo lokhudza katundu ndi chuma cha Pulezidenti, wachiwiri wake ndi nduna za boma ndi lokwanira, koma likusowekera nsanamira zake zimene anthu wamba angagwiritse ntchito polondoloza chumacho. Mkuluyu adafotokoza kuti poonjezera lamulo limene lilipo kale, Nyumba ya Malamulo iganizirenso zokhazikitsa lamulo lina lokakamiza atsogoleri kubweranso poyera ndi chuma chimene apeza pamene akuchoka mmaudindo awo. Kanyongolo akuti akadakonda mabungwe a Financial Intelligence Unit (FIU) ndi Malawi Revenue Authority (MRA) atapatsidwa mphamvu zounika mmene chuma cha atsogoleri chilili pamiyezi inayi iliyonse kapena pakutha pa chaka kuti Amalawi azidziwa ngati atsogoleriwa sakugwiritsa ntchito maudindo awo molakwika. Ndikunena izi chifukwa chipanda nkhani ya msonkho womwe mtsogoleri wakaleyu sanapereke ku MRA, dziko lino silikadadziwa kuti a Mutharika anali wolemera chonchi, Kanyongolo adatero. Katswiri wina pa zamalamulo, Justin Dzonzi, wati gawo 88 la malamulo a dziko ndi lopanda ntchito chifukwa silikupatsa mphamvu ndi chitetezo kwa nzika imene ikufuna kulondoloza momwe chuma cha atsogoleri chilili. Dzonzi adati ku Uganda nzika zili ndi mphamvu zofufuza atsogoleri awo mmene akugwiritsira ntchito udindo wawo komanso chuma cha boma. Koma mkulu wa bungwe la owerengera ndalama la Society of Accountants in Malawi (Socam) Evelyn Mwapasa akuti Amalawi atha kulondoloza katundu wa atsogoleri awo kudzera mmakalata ndi mapepala okhudzana ndi misonkho kuchokera ku MRA. Koma Mwapasa adatsindika kuti vuto lalikulu mdziko muno ndi kasungidwe ka mafayilo okhudzana ndi misonkho. Mmaiko ena, munthu sungapikisane nawo pampando wa pulezidenti kapena phungu wa ku Nyumba ya Malamulo pokhapokha utatulutsa umboni wosonyeza kuti umalipira msonkho, Mwapasa adatero. Iye adati pofuna kuthetsa katangale, bungwe lotolera msonkho liyenera kulimbikitsa ntchito yosunga mafayilo a misonkho. Ndipo akaona kuti atsogoleri athu akulemera modabwitsa, MRA ikuyenera kufufuza ndi cholinga choti wina asamadyere masuku pamutu Amalawi osauka, Mwapasa adatsindika. Mkulu wa Consumers Association of Malawi (Cama) John Kapito wapempha Amalawi kuti asataye nthawi kulimbana ndi chuma chimene Mutharika adazikundikira. Mmalo mwake, Kapito adati anthu akuyenera kukhala tcheru ndi boma la Peoples Party (PP) womwe akuti uli ndi kuthekera kowononga chuma chambiri ngati sipangapezeke njira zolitchingira. Si zodabwitsa kuti malemu Mutharika adapeza chuma chochuluka motere. Ifeyo ndi amene takhala tikumenya nkhondo yokakamiza atsogoleri kuti aulule chuma chawo, koma mmalo motithandiza pankhondoyi, tikutanganidwa ndi zinthu zina zopanda pake, iye adatero. ",11 "Osamalira Odwala Akhale Achifundo-Papa Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisko wati anthu omwe amasamalira odwala akuyenera kukhala achifundo. Iye walankhula izi mu uthenga wake wapa tsiku lomwe mpingo wa katolika pa dziko lonse umakumbukira odwala, lomwe ndi 11 February. Mu uthengawo, omwe mutu wake ndi Bwerani Inu Nonse Olema, Papa wati anthu osamalira odwala akuyenera kutengera chitsanzo cha Yesu Khristu pokhala achifundo. Papa wati Yesu Khristu akupereka uthenga wa chilimbikitsowu popeza kuti naye anadutsa mu mazunzo aakulu. Iye wati ngakhale sizikhala chomwechi mzipatala zambiri pa dziko lonse, komabe odwala akuyenera kulandira chisamaliro chokwanira. Mtsogoleri wa mpingo wa katolikayu wati mpingo ukuyenera kukhala msamaria wina wachifundo popereka chisamaliro kwa anthu odwala ndi ovutika mnjira zosiyanasiyana. Mpingo wa katolika umachita chaka chokumbukuira odwala onse pa 11 February tsiku lomwenso mpingowu umakumbukira amayi Maria aku Lourdes. ",14 " Gondwe azaza pamsonkhano Nduna ya za chuma Goodal Gondwe Lolemba idazaza pamwambo wosayinirana pangano la ngongole ndi banki ya zachitukuko mu Africa ya African Development Bank (AfDB) itazindikira kuti akuluakulu a kuundunawu sadabweretse mapepala osayinira panganolo. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndunayi imayembekezera kusayinira pangano la ndalama zokwana US$22 miliyoni (pafupifupi K16 biliyoni) mmalo mwa boma ndi oyimilira bankiyi Andrew Mwaba ku likulu la undunawu ku Lilongwe. Adakwiya: Gondwe Cholinga cha ndalamazi nkupititsira ntchito za ulimi patsogolo ndi kutukulira achinyamata paulimi. Gondwe adakhumudwa ndi kulephera kwa akuluakulu a kuundunawu kuzindikira kuti mwambowo udayamba palibe mapepala ofunikirawo ndipo adadula mkamwa oyendetsa mwambowo Alfred Kutengule kuti za mapepalawo zilongosoke. Zitheka bwanji kusayinirana pangano popanda mapepala ofunikira? Tisayina pati? Mapepala ali kuti apa? Adafusa Gondwe. Ndunayi itangolankhula izi, kudali yakaliyakali akuluakuliwo kuthamangathamanga mmawofesi kusaka mapepalawo kuti mwambo upitilire ndipo pomwe mapepalawo amapezeka, makina achinkuza mawu omwe amagwiritsidwa ntchito pa mwambowo adasiya kutulutsa mawu. ",11 " Ndidakamira kufunda nawo ambulera Padali pa 5 February 2014, kunja kuli mvula yamphamvu ya mabingu pomwe Devlin Nazombe kapena kuti Mmisiri Wopanda Zida yemwe amagwira ntchito ngati muulutsi kunyumba youlutsa mawu ya Angaliba komanso amaongolera zochitika monga zikwati ndi zina adakumana ndi mkazi wake Gloria Muhiwa. Ndipo Nazombe yemwe tsiku lina adaona koyamba Gloria atafunda ambulera kuphelera mvulayo. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Devlin ndi Gloria pa tsiku la ukwati wawo Apatu Nazombe sakadachitira mwina koma kumuimitsa namwaliyo nkumupempha kuti afunde nawo. Ndidamuimitsa kuti ndifunde nawo chifukwa ndidali ndikunyowa kwabasi. Nditamuimitsa adanyogodola koma sindidaimve, ndidakakamira kufikira pomwe adandiloleza kufunda nawo, adalongosola Nazombe. Komatu Nazombe sadapitire kufunda nawo ambulera kokha chifukwa adayamba kumupempha Gloria nambala yake ya lamya. Gloria adakanitsitsa kuti sangandipatse nambalayo. Koma ndidamukakamiza kuti chabwino angotenga nambala yanga ndipo adailemba mmanja kuti akakafika kwawo akaisunge, Nazombe adatero. Iye adawonjezera kuti atafika posiyana adamuchondelera namwaliyo kuti ayankhulane naye madzulo atsikulo chifukwa adali ndi chikaiko chachikulu. Koma Nazombe adati padadutsa sabata ziwiri asadamuyankhule ndipo adaiwalanso zoti adapereka nambala. Tsiku lina ndidaona uthenga woti ndiimbire munthu lamya ndipo nditamufunsa kuti ndi ndani adati Gloria, ndidabalalika kwambiri mpaka kufunsa kuti wakuti? Ndiye adandilongosolera kuti ndidamupatsa nambala yanga. Koma nditakumbukira, tidayamba kucheza, iye adatero. Patadutsa kanthawi awiriwo akucheza, Nazombe adamufunsira mkaziyo yemwe akuti adavuta kwambiri kuti amulole, komabe pamapeto pa zonse adavomera ndithu. Kuchokera nthawi imeneyo takhala tikukumana ndi zokhoma zochuluka monga chibwenzi kutha nkudzayambiranso; anzake amamuuza kuti sindingamukwatire chifukwa ndine wotchuka ndipo anthu otchuka sakhala ndi mkazi mmodzi koma chosangalatsa nchoti Gloria samazitengera zonsezo, Nazombe adalongosola. Koma awiriwo omwe amanga ukwati wawo pa August 31 pa mpingo wa South Lunzu CCAP ndipo madyelero adali ku Grace Garden ku Machinjiri, mumzinda wa Blantyre akulangiza anthu onse omwe ali mchikondi kuti asamamvere zokamba za anthu komanso chikondi chao chizikhala chotsogoza Mulungu kut mzonse azikula. Iwo adati akakumana ndi vuto lililonse amakhala pansi ndikukambilana modekha kuti wolakwa avomereze ndikupepesa ndipo zikatha amagwada pansi ndikumupempha Mulungu kuti awayanjanitse. Awiriwa amakhala ku Machinjiri mumzinda wa Blantyre ndipo Gloria amagwira ntchito ku sitolo za PEP komanso ali ndi salon komwe amamanga anthu tsitsi. ",10 " Anatchereza Ndikufuna kuchoka Zikomo Anatchereza, Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndidabwera kutauni kudzafuna ntchito ndipo ndidasiya mkazi wanga kumudzi. Ntchito ndidaipeza koma abale amene ndimakhala mnyumba yawo akuti ndisachoke kukafuna nyumba ya lendi ati sakufuna mkazi wangayo abwere. Kodi nditani kuti ndituluke mnyumba yawoyo? Thandizeni. Ine F. Zikomo a F, ndinu mwamuna kotero pena sibwino kumvera zilizonse. Apapa zikuonetseratu kuti abale anuwo samufuna mkaziyo. Ngati mkaziyo ali ndi vuto ndibwino anene kuti vutolo mulikonze, koma kumuletsa si yankho. Achibale ena amafuna kulowerera chilichonse chokhudza moyo wa munthu, pena ndibwino kuti munthu azikhala ndi ufulu wosankha chomwe akufuna komanso kuchita. Musalolere, ngati pali vuto kambiranani. Gogo, Ndili ndi mwana wa kunjira ndipo ndidakwatira mkazi wa mwana kale. Koma iyeyo adabweretsa mwanayo ine ndidasakudziwa ndipo chichitire izi, sakundilabadiranso. Nditani? Zikomo pa funso lanu lomveka. Choyamba ndifunse, kodi mayiwo adakuuzani kuti ali ndi mwana kunjira? Ngati sadakuuzeni ndiye kuti pali nkhani ziwiri, yoyamba imeneyo yachiwiri yoti abweretsa mwana mwa dzidzidzi. Bambo dziwani ichi kuti kholo lomwe aliyense amapanga zofuna zake silamoyo, kotero musalole kuti mpaka kude mutayambana ndi mkazi wanu. Mukhazikeni pansi ndipo akumasuleni nkhani yeniyeni. Ngati sakulankhula, kauzeni ankhoswe. Anatchereza, Ndili ndi zaka 28 ndipo ndili pabanja. Koma nthawi zonse ndikati ndikhale mchikondi ndi mkazi wanga, amanena kuti watopa. Ndingatani. M, Lilongwe. Zikomo bambo M, Tikati banja timanena kuchipinda, ngati wina akukana kulowa kuchipinda ndiye kuti akukaniza banja. Mumufunse kuti kuchipindako akumalowako ndi ndani? Zikuonetseratu kuti pali tambala wina amene asangalala mwa mayiyo. Kodi zavuta? Auzeni ankhoswe ndipo amasule bwalo pamene pali vuto. n Ndikufuna mwamuna Ndine mayi wa zaka 52, ndimakhala ku Dedza. Mwamuna wanga adamwalira mu 2003. Ndikufuna mwamuna amene angandikwatire koma akhale wopemphera. Chonde imbani 0992256715. ",12 "Ogwira Ntchito ku Ndende Ayamba Kunyanyala Ntchito Asilikali ogwira ntchito mmaudindo angonoangono mu ndende za mdziko muno ayamba kunyanyala ntchito pofuna kukakamiza boma kuti limve madandaulo awo. Malinga ndi mtolankhani wathu, kummawaku kunali mpungwepungwe ku Zomba Central Prison pakati pa asilikali a maudindo angonoangono ndi mabwana awo pomwe akuluakuluwo analawira kuyamba kugwira ntchito asilikali a maudindo otsika asanafike. Pamenepa asilikaliwa anathamangitsa mabwana awowa ndipo anatseka chipata cholowera ku ndendeyi moti padakalipano anenetsa kuti adzayamba kugwira ntchito madandaulo awo akamveka ndi kuyankhidwa bwino. Padakalipano apolisi omwe amatenga anthu oganiziridwa ku bwalo la milandu alephera kukatenga akayidi omwe amakhala akuyembekezera kupita ku khothi chifukwa chipata cha ndendeyi chinali chotseka. Malinga ndi malipoti, anthuwa akufuna ogwira ntchito a pansi kwambiri awakweze pa ntchito, awapatse ndalama zowonjezera chifukwa miyoyo yawo ili pa chiwopsezo ndi kubwera kwa mliri wa Coronavirus. Iwo akuti akufunanso kuti akuluakulu a ndende asiye kuchita tsankho, ponena kuti pali asilikali a ku ndende ambiri omwe akupindula chifukwa akuchokera mbali yomwe akuchokera akulu-akulu a nthambi-yi. Padakalipano wofalitsa nkhani za nthambi ya ndende mdziko muno Chimwemwe Shawa wati kunyanyala ntchito komwe akuchita asilikali otsika mmaudindowa ndi kosavomerezeka chifukwa sanatsate ndondomeko yake. ",14 " Alimbana ndi ntchemberezandonda ku Zomba Unduna wa zamalimidwe wati ntchemberezandonda zomwe zabuka mboma la Zomba zisatayitse anthu mtima chifukwa akatswiri apita kale mmadera omwe akhudzidwa ndi mbozizo. Mbozizo zapezeka kale mmadera ena mboma la Zomba mkulu wa zaulimi kumeneko Patterson Kandoje watsimikiza koma mneneri wa unduna wazamalimidwe Hamilton Chimala adati gulu la akatswiriwo likafikanso mmadera achigwa cha Shire. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Padakalipano nduna ndi gulu la akatswiri ali kale kalikiliki kulimbana ndi mbozizo ndipo iwo ndi amene angakhale ndi zonena zambiri pammene zinthu zilili, adatero Chimala. Ntchemberezandonda zimaononga masamba ofunika pokonza chakudya cha mbewu Nduna ya zamalimidwe Dr Allan Chiyembekeza adatsimikiza kuti iye pamodzi ndi akatswiri ali kalikiliki kulimbana ndi vutoli koma adati padakalipano sanganene kuti vutolo ndi lalikulu motani popeza akadali mkati mofufuza. Anthu angokhala ndi chikhulupiliro chifukwa akatswiri omwe akugwira ntchitoyo ndiwodziwa kwambiri moti ali ndi chikhulupiliro kuti vutoli silipita patali lisadagonjetsedwe, adatero Chiyembekeza. Ndunayo idati chongodandaulitsa chakuti mbozizo zimaononga kwambiri panthawi yochepa komanso vuto lake ndilakuti zimadya masamba omwe mbewu zimadalira popanga chakudya motero kakulidwe ka mbewu kamasokonekera. Ntizilombo tachabe kwambiri chifukwa timaononga masamba a mbewu choncho kuchedwa kutigonjetsa kukhoza kukhala ndi zotsatira zowawa kwambiri, adatero Chiyembekeza. Kandoje adati pamalo okwana mahekitala 34 omwe akhudzidwa, mahekitala 6 ndiwo adali atapoperedwa pofika Lachiwiri ndipo adapempha anthu kuti akhale tcheru kuti akangoona mbozi zobiriwira zokhala ndi mizere yoyera akauze a zaulimi chifukwa maonekedwe a ntchemberezandonda ndi wotero. Chiyembekeza: Tikuthana nazo Madera ozungulira malo a zaulimi a Mpokwa kwa T/A Mwambo makamaka midzi ya Saiti, Masambuka, Kwaitana, Mamphanda, Kabwere, Kumpatsa, Havala, Mlomwa ndi Chaima ndi ena mwa midzi yomwe yakhudzidwa. Ntchemberezandondazi zabuka panthawi yomwe alimi akudandaula kale ndi ngamba yomwe ikutha pafupifupi sabata zitatu tsopano ndipo mbewu zambiri zanyala kale mminda moti pali chiyembekezo choti ngambayi itati yapitirira ndiye kuti alimi akhoza kudzabzalanso. Ngambayo yadza kaamba ka mphepo ya El Nino yomwe yasokoneza magwedwe a mvula makamaka mmaiko a kummwera kwa Africa zomwe zapangitsa madera a mchigawo cha kummwera kwa Malawi akhudzidwe kwambiri. ",4 " Njengunje pothana ndi matenda a khansa Muli ntchito yaikulu mdziko muno kuti odwala matenda a khansa apeze mpumulo. Izi wanena ndi yemwe adapulumuka ku matendawa, Blandina Khondowe. Khondowe adaononga K5 miliyoni kuti apulumuke ndipo adachita kupita mdziko la India zitakanika kuti athandizidwe mdziko muno. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mpaka zafikatu pamenepa, amayi kufola pa mzere kuti ayezetse khansa Malinga ndi mkulu woyanganira ntchito za umoyo mu unduna wa zaumoyo Charles Mwansambo, zipatala za Kamuzu Central ndi Queen Elizabeth ndi zokhazo zomwe zili ndi ukadaulo wa matendawa. Kutanthauza kuti kupatula malowa, kulibenso kwina komwe wodwala angapite mdziko muno. Boma lidakhazikitsa ntchito yomanga malo wothandizita anthu odwala khansa mu 2007 koma mpaka pano malowa sadayambe kugwira ntchito. Kwa Khondowe, ili ndi vuto lalikulu lomwe likuika pachiopsezo odwala matendawa. Kupatula kuti tili ndi zipatala zochepa, vuto lina ndi la zipangizo, adafotokoza, ineyo ndidazindikira kuti bere langa limalimba mchaka cha 2011 ndipo kwa zaka ziwiri ndimayenda mzipatala koma amangondiuza kuti ndi chotupa, mpaka pamene ndidaganiza zopita ku India. Khondowe adaonjeza, nditapita ku India, ndidaononga K5 miliyoni. Ndi angati angakwanitse ndalama zoterezi? Pokhapokha titapereka mphamvu zambiri ku zipatala zathu, anthu apitirirabe kufa ndi khansa. Mmodzi mwa akadaulo pa matendawa, Leo Masamba adati pakali pano, chaka ndi chaka, anthu pafupifupi 18 000 amapezeka ndi khansa. Iye adati mwa anthuwa, amene ali pamoto ndi anthu akumudzi omwe chuma ndi chowavuta. Kuperewera kwa zipatala kukuzuza kwambiri anthu akumudzi chifukwa alibe ndalama kuti akapeze thandizo, adatero Masamba. Iye adati chofunika ndi kumema Amalawi kuti athandize boma kukwaniritsa pologalamu yokhazikitsa malo othandizirako anthu a vuto la khansa mzigawo zonse za dziko lino. Malinga ndi iye, mankhwala oyenera, zipangizo zogwirira ntchito, ogwira ntchito odziwa bwino ndi galimoto zokwanira zonyamula anthu osowa mayendedwe ndi zinthu zomwe zikufunikira. Akatswiri pa za umoyo ati pokhapokha patachitika chozizwa, Amalawi apitilira kupululuka ndi matendawa chifukwa cha kusowekera kwa zipangizo komanso zipatala. Mkulu woyanganira nthambi yothandiza ku matenda a khansa pa chipatala cha Kamuzu Central, Richard Nyasosela wati chipatalachi chimalandira anthu osachepera 30 sabata iliyonse. Steady Chasimpha wa ku nthambi yowona za matenda a khansa wati ku Queen Elizabeth Central Hospital, anthu ofuna thandizo sachepera 22 pa sabata imodzi. Iye wati nambala zochuluka chotere nzowopsa poyerekeza kuchepa kwa ogwira ntchito ku nthambi za khansa ndi zipangizo zothandizira anthu ovutikawo. Nambala imeneyi ikusonyeza kuti zinthu sizili bwino, ndipo tikatengera vuto la ogwira ntchito ndi zipangizo, thandizo loperekedwa silingakhale loyenera, adatero Chasimpha. Kusowekera kwa zipatala kwachititsa kuti anthu ena mmidzi azipita kwa asinganga kukalandira thandizo. Mtsogoleri wa asinganga mdziko muno, Frank Manyowa akuti patsiku amalandira anthu pafupifupi asanu atatu odwala khansa. Ambiri mwa anthuwa sapulumuka chifukwa asingana ena amangofuna adyepo ngakhale sangakwanitse, adatero. Anthu pafupifupi 52 ndiwo amapezeka ndi matenda a khansa pa sabata mdziko muno, pakutha pa mwezi, anthu pafupifupi 204 ndiwo amapezeka ndi matendawa. Koma Khondowe akuti kutengera zomwe madotolo adamuuza ku India, khansa ndiyochizika ikapezeka mmasiku oyambilira komanso thandizo loyenera likakhala pafupi. Apo ayi ndiye amakangodula chiwalo mukachedwa kulandira thandizo. Lero Khondowe adayambitsa bungwe la Think Pink lomwe limapita mmadera osiyanasiyana kuphunzitsa anthu za khansa ndi kuwalimbikitsa kuti azikayezetsa. ",6 " Chifunga pa za boma la fedulo Nkhungu yowirira yakuta tsogolo la boma la fedulo (Federalism) lomwe magulu ena mdziko muno akufuna pamene ena sakugwirizana ndi maganizo otero. Maganizo a boma la fedulo adabwera chifukwa choti anthu ena akuganiza kuti pali tsankho pa kagawidwe ka maudindo ndi chitukuko mdziko lino. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Jessie Kabwila Mbusa Peter Mulomole, yemwe ndi mneneri wa bungwe la anthu a chipembezo la Public Affairs Committee (PAC) lomwe lidasankhidwa ndi boma kuti limve maganizo a wanthu pa za boma la fedulo, wati anthu akusiyanabe maganizo pankhaniyi chomwe chikusonyeza kuti ambiri sakudziwabe tanthauzo la boma la fedulo. Iye adati ichi ndi chipsinjo ku bungwe la PAC. Takhala tikugwira ntchito yofufuza maganizo a anthu pa nkhaniyi kuyambira mwezi wa November chaka chatha koma mpaka pano tsogolo lenileni silikuwoneka chifukwa tikulandira maganizo osiyanasiyana, adatero Mulomole. Iwo adati akumanapo ndi magulu osiyanasiyana mchigawo cha pakati komwe adamva maganizo osiyanasiyana ndipo padakali pano ali mchigawo cha kumpoto komwenso magulu osiyanasiyana akupereka maganizo awo. Tikukumana ndi mafumu, a mipingo, mabungwe, andale, amabizinesi, ogwira ntchito mboma ndi mmakampani komanso akatswiri mmagawo osiyanasiyana monga zandale, zachuma ndi zamalamulo. Anthu amenewa akutiwuza maganizo awo mosaopa, adatero Mbusa Mulomole. Mneneriyu adati anthu asayembekezere zotsatira msanga chifukwa nkhaniyi ndiyokhudza dziko lonse choncho nkofunika kuti bungweli litolere maganizo a anthu mofatsa nkupeza chenicheni chomwe akufuna. Mulomole wakana mphekesera zoti boma ndilo likupereka ndalama zopangitsira misonkhanoyi. Iwo adati ngati mbali imodzi yokhudzidwa pa nkhaniyi, boma likadapereka ndalama kubungwe la Pac zoti ligwirire ntchitoyi, zotsatira zake sizikadapereka tanthauzo. Ife ngati bungwe loyima palokha, sitikutenga mbali ili yonse pa nkhaniyi. Ntchito yathu ndiyongofufuza zomwe anthu akufuna; choncho sitikuyenera kulandira ndalama zogwirira ntchitoyi kuchoka ku mbali ili yonse yokhudzidwa, adatero a Mulomole. Iwo adapitiriza kunena kuti bungwe lawo pamodzi ndi bungwe la chi Katolika lowona za chilungamo la Catholic Commission for Justice and Peace (CCJP) akugwira ntchitoyi ndi thandizo lochokera ku bungwe la United Nations Development Programme (UNDP). Nkhani ya fedulo idadzetsa mtsutso waukulu kuyambira miyezi ya August ndi September chaka chatha pamene mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika adasankha nduna zake zomwe zambiri zidachokera mchigawo cha kummwera. Zipani zotsutsa boma ndi magulu ena, makamaka a mchigawo cha kumpoto ndi pakati, adati kuli bwino dzikoli litagawidwa kutengera zigawo ndi cholinga choti chigawo chiri chonse chidzidzipangira chokha ndondomeko za chitukuko. Phungu wa dera la Hora mboma la Mzimba a Christopher Ngwira komanso wa dera la kuvuma mbomalo a Harry Mkandawire, omwe ndi a chipani cha Peoples Party (PP), ndi ena mwa anthu omwe adayambitsa komanso kulimbikitsa maganizo a boma la fedulo. Chipani cha Malawi Congress Party (MCP) nachonso chidagwirizana ndi maganizo oyambitsa boma la fedulo. Mneneri wa chipanichi a Jessie Kabwila adati boma la fedulo lidzapangitsa kuti madera onse a dziko liko atukuke. Kafukufuku yemwe Tamvani adapanga adasonyeza kuti aphungu ambiri aku nyumba ya malamulo sakugwirizana ndi maganizo oterowo kamba koti atha kugawa dziko. Koma boma lidati anthu apatsidwe mwayi wonena zakukhosi kwawo ngati akufuna boma la fedulo kapena ayi. Boma silikufuna kupondereza maganizo a wanthu pa nkhani ya boma la fedulo. Aliyense ali ndi ufulu opereka maganizo ake koma izi zichitike poganizira udindo omwe munthu aliyense ali nawo, adatero a Kondwani Nankhumwa, omwe ndi mneneri wa boma. Pogwirizana ndi a Mulomole, a Nankhumwa adati boma sililowelera pa ntchito yomwe bungwe la PAC likuchita yophunzitsa anthu kapena kufufuza maganizo awo pa za boma la fedulo. A Nankhumwa adatinso boma silidaperekeo ntchitoyi mmanja mwa bungwe kapena nthambi ili yonse koma lidangotsegula chitseko kwa mabungwe ndi ena omwe angakwanitse kuphunzitsa anthu kuti adziwe ubwino ndi kuyipa kwa boma la fedulo. Bomatu silidakane kapena kuvomereza boma la fedulo, koma kuti anthu apereke maganizo awo komanso aphunzitsidwe mokwanira. Ichi ndi chifukwa tidalekera mabungwe omwe angakwanitse kuti agwire ntchitoyi ndi ndalama zawo, adatero Nankhumwa. Koma a Ngwira adati akukaika kuti boma lili ndi chidwi pa nkhani imeneyi. Tawonapo nkhani zikuluzikulu zikufera mmazira ngakhale komiti yoona nkhanizi itakhazikitsidwa. Kukadakhala kuti boma liri ndi chidwi, likadapereka chithandizo choti anthu omwe akugwira ntchitoyi agwiritse, adatero a Ngwira. Polankhula ndi Tamvani, katswiri wa zandale ku sukulu ya ukachenjede ya Chancellor College a Blessings Chinsinga adachenjeza kuti nkhani ya boma la fedulo siyofunika kupupuluma. A Chinsinga adati nkhaniyi ndiyofunika iyende mundondomeko zingapo isadafike pokhazikitsidwa choncho mpofunika kuunika bwino kuti zinthu zidzayenda motani bomalo likadzavomerezedwa. Choyamba, anthu akufunika kuphunzitsidwa za tanthauzo la boma la fedulo ndi cholinga choti apereke maganizo awo pachinthu chomwe akuchidziwa bwino. Zikatero, ngati anthu avomereza, pakuyenera kukhala voti ya liferendamu. Pofika popangitsa chisankho cha liferendamu, palinso zofunika kuchita zingapo monga kuunika mmene chuma chizigawidwira, komanso mmene malamulo aziyendera monga kukhala ndi malamulo amodzi dziko lonse kapena chigawo chiri chonse chikhale ndi malamulo ake zomwe sizapafupi, adatero Chinsinga. ",11 " Tadeyo Mliyenda: Ulendo wa ku Mzuzu Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Tsikulo Abiti Patuma adandipeza pa Wenela kuti ndimuperekeze ku Mzuzu kumene amakacheza ndi Paparazzi komanso anzake. Tidakwera basi yausiku pa Wenela monga mudziwa kuchoka pa Wenela kukafika ku Mzuzu ndi mtunda wautali zedi. Mudali kuphulika nyimbo za mnyamata uja woukira, Jaso, inde mnyamata amene aliyense akudziwa bwino kuti amacheza kwambiri ndi Mpando Wamkulu koma lero akuti sakufuna kumvana Chichewa ndi mdzukulu wake wa Mpando Wamkulu, inde Atipatsa Likhweru. Chilipo chikuchitika kuti lero lino Jaso azioneka kuti akuukira Atipatsa Likhweru ndi anzake ena onse ku Ukafuna Dilu Fatsa. Ulendo uli mkati, Abiti Patuma adayamba kukamba zodziwa yekha. Palibe icho ndimatola pankhani zimene iye amakamba. Komatu zinaliko uku ku Kanjedza. Paja mudziwa Lazalo Chatsika uja wa Male Chauvinist Pigs masiku apitawa anamuuziratu Moya Pete kuti zomwe ananena zimakhala ngati zonena mlezi. Ndiye anyamata a Dizilo Petulo Palibe anamutengetsa ku Kanjedza, kufuna kumumenya, adali kutero Abiti Patuma. Palibe icho ndidatolapo. Koma ndiye kunali kukwenyana anyamata, kutsala pangono kutulutsirana nkhwangwa, adapitiriza. Abale anzanga, zovuta kumvetsa izi. Tidayenda ulendowo bwino lomwe ndipo pa Jenda tidafika cha mma 2 koloko usiku. Chilankhulo chidayamba kusintha. Mpando wathu tidakhala anthu atatu. Kuwindo kudali Abiti Patuma, ine pakati ndipo mbali inayi kudali mkulu wina amene ankaoneka kuti wangofika kumene kuchokera ku Joni. Mkuluyo adandifunsa: Kasi mukuluta nkhu? Ndidamvapo nthawi ina kuti apa akutanthauza kuti mukupita kuti? Ine kuyowoya Chitumbuka nikuyowoya koma kweni kuti nipulike, nikutondeka chomene, ndidayankha. Ambiri mubasiyo adali mtulo. Kamphepo kadali katawakokera kutulo. Mwadzidzidzi, tidamva wina akukuwa: Choka! Choka! Iwe choka! Mayooooo! Aliyense mubasimo adadabwa kuti chikuchitika nchiyani. Ngakhale amene amagona adadzidzimuka. Mkulu uja adadzidzimukanso kutulo kwakeko ndipo tonse tidaseka chikhakhali. Atafunsidwa kuti amalota chiyani, iye adangoti: Ndimalota anthu a mapazi ngati nkhwangwa komanso malilime ngati mipeni, adayankha mkulu uja. ",15 " ANatchereza Sakufuna kukaonekera Gogo Natchereza, Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Mnyamata wina adandifunsira chibwenzi ndi cholinga choti tidzakwatirane. Padakali pano padutsa zaka zinayi tili paubwenzi, koma palibe chomwe amandiuza chokhudza ukwati. Mnzangayu amangofuna tizigonana basi. Gogo ndithandizeni. Kodi ndimutaye mnyamatayu? TTK TTK, Mutaye! Mnyamatayu zomwe akufuna nzongogonana basi osati za banja. Anyamata ambiri amabwatika atsikana powauza kuti adzawakwatira koma akudziwa kuti zaukwati ali nazo kutali. Chakumtima kwawo chikaphwa, atsikana aja samawawerengeranso. Nawo atsikana vuto lawo lalikulu nkutengeka poganiza kuti akakana kugona nawo awasiya nkukapeza ena. Apatu ine ndikuona kuti mnyamatayu ndi kamberembere. Mutaye asakutaitse nthawi yako pachabe. Gogo Natchereza Bwenzi langa chimasomaso Gogo Natchereza, Ndidakumana ndi mtsikana wina mu mzinda wa Mzuzu zaka zitatu zapitazo, tidapatsana nambala za foni ndipo takhala tikuimbirana mpaka ubwenzi udayamba. Mtsikanayu amagwira ntchito pa ku banki ina mu mzindawo moti ali ndi mnyumba yakeyake yomwe amakhala. Gogo, mnzangayu ndamupezapo katatu konse ali pa chikondi ndi amuna osiyanasiyana, koma wakhala akundipempha kuti ndimukhululukire ndipo ine ndimakhululukadi. Gogo, mtima wanga ndiwosweka chifukwa mnzangayu ndimamukonda kwambiri moti maganizo, moyo ndi mphamvu zanga zonse zidali pa iye. Nditani, gogo? Chonde ndithandizeni! HKA HKA Mtsikanayu ndi njinga simungapitirire kukhala naye paubwenzi. Mutha kutero mwakufuna kwanu, koma mudzanongoneza bondo mtsogolo muno chifukwa khalidwe la chimasomaso sindikuona akusiya. Ngati akuchita ukathyali muli paubwenzi, zidzatha bwanji mukadzamukwatira? Ndikudziwa kuti nzopweteka kusiyana ndi wokondedwa wanu, koma limbani mtima. ",12 "Zipani za MCP, UTM Zadzudzula Boma Kamba Kotayilira pa Nkhani ya Coronavirus Mgwirizano wa zipani za UTM ndi MCP wadzudzula boma kaamba kolephera kukwaniritsa ndondomeko zoyenera zomwe zikuyenera kuchitika kusanachitike mbindikiro ofuna kuchepetsa kufala kwa nthenda ya COVID-19 mdziko muno. Chikalatachi chati masiku asanu ndi awiri omwe bungwe la Human Rights Defenders Coalition (HRDC) komanso anthu ena anatenga chiletso choyimitsa ganizoli, unali mpata oti boma likonze ndondomeko zoyenera pokonzekera mbindikirowu. Boma lalephera kuika njira zina zomwe zingapangitse kuti nthendayi isafale kwambiri mdziko muno komanso kulephera kukhazikisa komiti yoti iwunike bwino za nthendayi, chatelo chikalatacho. Padakalipano Judge Kenyatta Nyirenda yemwe amamva nkhani yokhudza chiletsochi wati azapereka chigamulo chake pa nkhaniyi lachitatu likudzali. ",11 "Mdipiti wa Galimoto za Chilima Wachita Ngozi; Anayi Afa Anthu anayi afa ndipo awiri avulala pa ngozi yomwe yachitika kwa phalula mboma la Balaka. Malinga ndi mneneri wa apolisi mboma la Balaka Inspector Felix Misomali, imodzi mwa galimoto za pa mdipiti wa wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino yagundana ndi galimoto ina mu nsewu wa Zalewa. Imodzi mwa galimoto zapa mdipitiwo Iye wati ngoziyi siyinakhudze wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko linoyu kaamba koti galimoto yake inali itadutsa kale koma yomwe inachita ngoziyi ndi galimoto yomwe inali kumapeto kwa mdipitiwu. Galimoto ya mtundu wa Toyota Vitz Saloon nambala yake BW 8173 yomwe amayendetsa ndi Tamara Kamanga imadutsana ndi convoy ya Vice president koma chifukwa choti imathamanga kwambiri dalaivalayu analephera kuwongolera bwino galimotoyo zomwe zinachititsa kuti akawombane ndi galimoto yomwe inali kumapeto kwenikweni kwa mdipiti umene wa Vice President-wu, Toyota Rand Cruiser nambala yake BW1732 momwe munali dalaivala ndi wapolisi mmodzi, anatero Inspector Misomali. Inspector Misomali ati kutsatira ngoziyi amayi awiri omwe anakwera galimoto ya Vitz yi omwe sakudziwika mayina awo, afera pa malo a ngoziwo komanso bambo wina yemwe anali mu galimoto yomweyo wamwalira atangofika naye pa chipatala cha Phalula ndipo pamapeto pake dalaivala wa galimotoyo wamwalira atafika ku chipatala cha boma la Balaka. Anthu awiri omwe anali mu galimoto yapa mdipitiwo avulala ndipo padakalipano awatengera ku chipatala cha Kamuzu Central mu mzinda wa Lilongwe. ",14 "Anthu 10 Apezeka ndi Coronavirus, Chiwerengero Chafika pa 33 Nduna ya zaumoyo a Jappie Mhango omwenso ndi wapampando wa komiti yapadera yowona za matenda a COVID-19 alengeza kuti anthu ena khumi 10 apezeka ndi matenda a COVID-19 mdziko muno. Malingana ndi Mhango, anthu onsewa ndi ochokera kwa Kaliyeka mu mzinda wa Lilongwe, zomwe zafikitsa chiwelengero cha anthuwa pa 33 pomwe atatu amwalira, enanso atatu achira ndipo anthu omwe padakali pano akudwala matendawa ndi okwana 27. Malinga ndi kafukufuku yemwe wachitika poyeza anthuwa, apeza kuti anthuwa anali pafupi kapena anakhudzana ndi mmodzi mwa odwala yemwe wamwalira dzulo ndi matendawa mu mzinda wa Lilongwe. ",6 "Papa Wapempha Akhristu Kukhala a Chikhulupiriro Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wati akhristu akuyenera kuyika chikhulupiliro chawo mwa Mulungu yemwe ndi wa chifundo komanso wa chilungamo. Papa Francisko Papa Francisco walankhula izi lolemba pa Misa yomwe watsogolera ku likulu la mpingo-wu ku Vatican. Iye wati ndi koyenera kuti akhristu azikumbukira kuti ngakhale amachimwa, mulungu ndi wa chifundo komanso wa chilungamo. Papa Francisco wati Mulungu ndi wa chifundo komanso wa chilungamo ndipo amasintha anthu oipa kukhala anthu abwino. Mwazina pa misayi Papa Francisco wapempherera onse omwe adzadzidwa ndi mantha chifukwa cha nthenda ya Covid-19 yomwe yakhudza dziko lonse lapansi ndipo wakumbutsa anthu kuti Mulungu sataya anthu ake koma amakhala nawo nthawi zonse. ",13 "Zokonzekera za Mayeso a Katekisimu wa Ana Zatha Zokonzekera za mayeso a Katikisimu wa ana a Tilitonse omwe akuyembekezeka kuchitika loweruka pa 16 May kudzera pa Radio Maria Malawi, ati zafika kumapeto tsopano. Mkulu wa mu oofesi yowona za mabungwe a utumiki wa a Papa mdziko muno ya Pontifical Mission Societies (PMS) bambo Vincent Mwakhwawa, anena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi mu mzinda wa Lilongwe. Iwo ati pakadali pano ofesi yawo yomwenso yakonza mayesowa,yaika chilichonse chofunikira patsikuli kuti lidzakhale lopambana kwa anawa. Zokonzekera mayeso a ana omwe akuyembekezereka kuchitika pa 16 May zafika pamapeto ndipo mayesowo takonza komanso mphatso tayika mchimake, anatero bambo Mwakhwawa. Iwo apempha makolo komanso ana kuti akonzekere bwino powerenga zomwe anaphunzira komanso makolo powagulira ma units okwanira kuti azatenge nawo gawo pa tsikuli. ",13 " Maneb ikhutila ndi mayeso a sitandade 8 Bungwe loyendetsa mayeso la Malawi National Examinations Board (Maneb) lati lakhutira ndi mmene mayeso a Sitandade 8 ayambira. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mkulu wa bungweli Roy Hauya adanena izi Lachinayi atayendera malo angapo komwe ophunzira amalembera mayeso kuyambira Lachitatu. Lachitatu Hauya adayendera sukulu zina ku Blantyre ndipo Lachinayi adali ku Lilongwe. Takondwa ndi mmene mayeso ayambira. Nditsimikizire dziko lonse kuti mayeso akuyenda bwino. Anzathu achitetezo akugwira ntchito yawo bwino ndipo ophunzira akulemba momasuka.Tikufuna zipitirire chonchi Mmene tikhale tikuyamba mayeso ena mwezi ukubwerawu,adatero Hauya. Koma iye adavomereza kuti alandira lipoti lochokera mboma la Mchinji loti munthu wina amalembera wophunzira wina mayeso. Pakadalipano tingati talandira mlandu umodzi wa mayesowa.Wolembera mnzake mayeso amugwira ku Mchinji, adatero Hauya. Ophunzira adamaliza mayeso awo dzulo Lachisanu. ",3 " Zikhulupiriro zina Zisokoneza mdulidwe Zikhulupiriro zosiyanasiyana zikusokoneza ntchito ya mdulidwe wa abambo womwe unduna wa zaumoyo komanso mabungwe akulimbikitsa, Msangulutso wapeza. Escom in free-for-all fuel scam Wait gets longer Secrecy over party funders Ku Nsanje, Dowa komanso ku Nkhata Bay ndi maboma ena amene zikhulupirirozi zachititsa kuti abambo asamapite kuchipatala kukalandira mdulidwewu. Malinga ndi Senior Chief Dzoole ya mboma la Dowa, anthu ati samvetsa komwe kumapita kachikopa kamene adulako, zomwe zimawapatsa mantha. Anthu amaganiza kuti kachikopa kamene akadulako amakakachitira mankhwala. Maganizo awa ndi amene amachititsa anthu kuno kuti asapite kukalandira mdulidwe. Komanso anthu okwatira amaganiza kuti pamene akalandira mdulidwe, ndiye kuti akazi awo aziwayenda njomba chifukwa akawadula sangakakhale malo amodzi ndi mkazi wawo, ati panthawi iyi amaganiza kuti mkazi wawo akhoza kuawayenda njomba, adatero Dzoole. Mdulidwe wa abambo wakuchipatala ndi njira imodzi yothandiza kupewa kufala kwa HIV Dzoole adati mdera lake, mwa amuna 10, amuna anayi okha ndi amene amalandira mdulidwe. Kampeni ili mkati moti mafumufe atiphunzitsa kuti timeme anthu akachititse mdulidwe, koma ndi amuna ochepa amene akupita kukalandira mdulidwe, adatero Dzoole. Senior Chief Kabunduli wa mboma la Nkhata Bay wati kampeniyi yakanika kumeneko chifukwa anthu amaganiza kuti akakalandira mdulidwe ndiye kuti alowa chipembedzo cha Chisilamu. Ambiri kunoko amaganiza kuti amene alandira mdulidwe ndiye kuti ndi achipembedzo cha Chisilamu. Maganizo amenewa ndi amene akuchititsa kuti anthu asakhale nazo chidwi zokalandira mdulidwezo, adatero Kabunduli. Titafunsa mfumuyi ngati ikumemeza anthu ake kuti akachititse mdulidwe, iyo idati: Ukawauza kuti kachitsitseni mdulidwe, akufunsa ngati iweyo unapanga. Ndiye ine pa msinkhu wangawu sindingapite kumdulidwe. Ndinetu munthu wamkulu, ndiye ndikakalandira mdulidwe lero, balalo lidzapola liti? ..sindingapange zimenezo komanso kampeni imeneyi ine sindikuchita nawo. Ku Nsanje, malinga ndi McKnowledge Tembo, HIV/Aids co-ordinator pachipatala cha boma, zikhulupiriro za anthu kumeneko zimati munthu akalandira mdulidwe ndiye kuti amaafooka kuchipinda. Kunoko tinaphunzitsa mafumu, amipingo ndi azaumoyo za ubwino wa mdulidwe, koma mukamayenda muja, anthu amafunsa zambiri zokhudza zikhulupiriro zawo ndi mdulidwe. Palibe amene adabwera poyera kudzatiuza kuti akufooka kuchipinda chifukwa walandira mdulidwe. Komabe anthu upeza akulankhula, ndi zabodza ndipo palibe umboni wake. Zoona zake nzoti macheza amakhalanso bwino mbanja mwamuna akakhala kuti adalandira mdulidwe, adatero Tembo. Nayenso Simeon Lijenje wa PSI akuti ndi bodza la mkunkhuniza kuti amuna amene alandira mdulidwe amafooka ndipo wati amuna amene adulidwa ndiwo amachitanso bwino kuchipinda kusiyana ndi osadulidwa. Palibe umboni wa zomwe anthuwo akunena. Dziwani kuti mwamuna amene walandira mdulidwe ndiye amasangalala kuchipinda chifukwa amakwaniritsa bwino chilakolako cha mkazi wake, adaphera mphongo Lijenje. Iye adati kampeni ya mdulidwewu idayamba mu 2012 ndipo kuchokera mu October 2014 mpaka September 2015 pafupifupi abambo 93 642 ndiwo alandira mdulidwe mbomalo. Achipatala amati ngati abambo alandira mdulidwe, ndiye kuti pali mwayi woti chiwerengero cha anthu otenga kachilombo ka HIV podzera mkugonana chingachepe ndi anthu 6 mwa 10 alionse (60%), malinga ndi mabungwe a WHO komanso UNAIDS. Kuyambira mu 2007, mabungwewa akhala akubwekera kuti mdulidwe umathandize kwambiri kuti kachilomboka kasafale kwambiri. Malinga ndi mabungwewa, maiko 14 a kummwera kwa Afrika komanso kummawa, ndiwo ali kalikiriki kupangitsa kampeni kuti amuna azikalandira mdulidwe. Mdulidwe wa abambo ndi pamene achipatala amadula kachikopa kakutsogolo kwa chida cha abambo. Kachikopaka kamasunga zoipa, koma ngati walandira mdulidwe, amakhala waukhondo. Zoipazo zimakhala zasowa malo oti zisungidwenso, lidatero lipoti la UNAids, nkuonjera kuti mdulidwe umathandiza kuchepetsa matenda a khansa ya khomo la chiberekero cha amayi. ",15 " DPP, Kasambara trade barbs, witnesses scared There was drama in the High Court in Lilongwe yesterday when a former student and her lecturer locked horns across the divide of the prosecution and defence in the ongoing Paul Mphwiyo shooting trial. Private practice lawyer and accused person Ralph Kasambara and Director of Public Prosecutions (DPP) Mary Kachale exchanged tough words, with the former minister of Justice and Constitutional Affairs accusing the prosecution of personal persecution. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Kachale (L): The allegations are far from the truth Kasambara belittled Kachales concerns that he and other accused persons had intimidated State witnesses who, she said, fear for their lives. But Kasambara said the DPP was just being dramatic. Said Kasambara: The drama being played by the DPP is obvious. She knew she was dealing with elusive witnesses. All this is for dramatic effect to castigate us. All this is intended to play with the public and the media, all just to attack me. He alleged that a police officer from Blantyre, Alex Phiri, had been making night phone calls threatening his wife and brother-in-law with prosecution if they did not comply to testifying against the senior counsel, but Kachale vehemently denied the allegations. Kasambara during an earlier court appearance Kasambara further accused Kachale of favouring another accused person, Oswald Lutepo, who is not subject of bail revocation. She shot back that as her former boss and trainer, she had a lot of respect for Kasambara; hence, she could not have a personal vendetta against him. This [prosecuting Kasambara] was not an easy decision for me to take, but I took it. The allegations he is making here are far from the truth. We do not intend, as the State, to call his wife as a State witness. These serious allegations are casting a slur on my character as well, Kachale charged back. On allegations of favouring Lutepo, Kachale said if he were her favourite, she would not have added him to the case once she examined the evidence and affidavits when she came into the office of the DPP. Kachale insisted that the prosecution had evidence to show witness tampering, but in the meantime, they would ask the court to subpoena them to appear in court by force even though they might become hostile witnesses. Another defence lawyer, John-Gift Mwakhwawa, intervened in the heated exchange and recommended that the State should use the machinery at its disposal to bring the State witnesses to court. Earlier, the DPP told the court that State witnesses were not willing to testify against the six accused persons, claiming that they fear for their lives. Some of the witnesses have been given police protection, but they said they are still afraid to testify against Kasambara, Macdonald Kumwembe and Pika Manondo who are answering charges of attempted murder and conspiracy to commit murder. Kachale said she was forced to ask for an adjournment after the witnesses lined up to testify, including a Chalunda and Defeneya, a ballistics expert from the Malawi Police Service, a police investigator and officials from Airtel Malawi who have since been withdrawn as witnesses. Chalunda and Defeneya approached the prosecution and recorded statements in which they made allegations of intimidation from the accused persons only to change tact and claim that the prosecution was forcing them to change witness statements. She added that the prosecution had concrete evidence to show the level of intimidation the witnesses have undergone. Presiding High Court judge Michael Mtambo is yet to make a ruling on an application to revoke bail for the accused persons who she accused of engaging in mafia-like operations to intimidate witnesses and prevent them from testifying against them. The other accused persons are Dauka Manondo, Lutepo and Robert Kadzuwa whose bail has since been revoked for failing to show up for trial for two consecutive sessions. ",11 "Papa Akuyembekezeka kuchita Misa Yopemphelera Anthu Othawa Kwawo Wolemba: Glory Kondowe Mtsogoleri wa mpingo wa Katolika pa dziko lonse Papa Francisko lamulungu wati anthu ndi mayiko akuyenera kumadzipereka pothandiza anthu othawa kwawo. Papa walankhula izi ku likulu la mpingowu ku Vatican. Mwazina Papayu wakumbutsa anthu kuti la mulungu likubwera-li pa 29 September ndi tsiku la nambala 105 lokumbukira anthu othawa kwawo kotero akuyenera kukonzekera bwino kuti tsikuli lidzakhale latanthauzo. Papa wati adzakumbukira tsikuli pa mwambo wa msembe ya Misa yomwe adzatsogolere pa bwalo lalikulu la SAINT PETERS SQUARE ku likulu la mpingowu ku Vatican. ",13 " Osabweza ngongole ya Mardef ali mmadzi Anthu amene sadabweze ngongole ya Malawi Enterprise Development Fund (Mardef) ali mmadzi pamene ayamba kuona zakuda. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ngongole ya Mardef idayamba nthawi ya ulamuliro wa Bingu wa Mutharika pomwe amapereka ndalama kwa achinyamata kuti ayambire bizinesi. Koma ambiri mwa anthuwo sanabweze ngongoleyo. Malinga ndi anthu ena amene tacheza nawo mboma la Kasungu, anthu amene sadabweze ngongoleyi ayamba kumangidwa pamene ena akuwalanda katundu. Mneneri wa Mardef Isaac Mbekeani watsimikiza kuti bungwe lawo layamba kutoleradi ngongoleyo mboma la Kasungu ndi maboma ena. Koma iye adati timupatse mpata kuti afufuze kuchuluka kwa anthu amene akuwafufuza ngakhalenso ndalama zimene zikufu nika. Tumizireni mafunso ndipo ndikuyankhani tsatanetsatane wake za nkhaniyi, adatero Mbekeani Lachinayi koma pofika Lachisanu nkuti asadayankhe mafunsowo. Koma nyakwawa Alamu ya pamsika wa Nkhamenya adatsimikizira Msangulutso kuti anthu ena anjatidwa koma sadapereke zambiri pankhaniyi. Mmudzi mwanga mulibe amene ali ndi ngongoleyi chifukwa iwo amene adakongola nawo adabweza kale ngongoleyo, koma madera ena mboma lino ndiye anthu ali pakalapakala, idatero mfumuyo. Mayi ena amene sadafune kutchulidwa koma akukhala pamsika wa Nkhamenya mbomalo, adati anthu amene sadabweze ngongoleyi ayamba kubisala. Pamene zidamveka mwezi watha kuti amene sadabweze ngongoleyi ayamba kuwamangitsa, anthu ena asamuka kuno pamene ena akumabwera usiku wokhawokha ndi ena athawiratu. Ngati sudabweze ngongoleyi akumakumangitsa, apo ayi ena akumawatengera zinthu monga mwa mgwirizano wa ngongoleyo, adatero. amene adakongola nawo adabweza kale ngongoleyo, koma madera ena mboma lino ndiye anthu ali pakalapakala, idatero mfumuyo. Mayi ena amene sadafune kutchulidwa koma akukhala pamsika wa Nkhamenya mbomalo, adati anthu amene sadabweze ngongoleyi ayamba kubisala. Pamene zidamveka mwezi watha kuti amene sadabweze ngongoleyi ayamba kuwamangitsa, anthu ena asamuka kuno pamene ena akumabwera usiku wokhawokha ndi ena athawiratu. ",2 "Chipani cha Sacramentine Chichita Chaka cha Asisteri Atatu Wolemba: Thokozani Chapola Chipani cha asisteri cha Sacramentine chachita chaka pomwe asistweri awiri amalumbira malumbiro a ku nthawi zonse pomwe sisteri mmodzi amakondwelera kuti wakwnitsa zaka 50 akuctumikira mulungu ngati sisteri mu chipanichi. Sister Francesca Cortinovice a mdziko la Italy akwanitsa zaka 50 mu utumiki komanso Sister Veronica Chilemba ndi Sister Theresa Misomali alumbira malumbiro a ku nthawi zonse. Mwambowu unachitikira ku parishi ya Ntcheu mu dayosizi ya Dedza ndipo anatsogolera mwambowu ndi mkulu woyendetsa ntchto za dayosiziyi bambo John Chithonje. Mmawu awo bambo Chithonje alangiza makolo kuti atengerepo chitsanzo cha asisteriwa polimbikitsa ana awo pa nkhani ya maphunziro. Zipani zikamatenga ana oti alowe mu chipani, chimodzi mwa zinthu ziomwe amayangana ndi sukulu yomwe anachita. Choncho makolo akuyenera kulimbikitsa ana awo pa maphunziro, anatero bambo Chithonje. Mmodzi mwa akuluakulu a chipani cha sacramentine kuno ku malawi sister hellen matchado ati iwo ndi okondwa kuti mwambowu watheka ndipo wapempha asisteriwa kuti akhale odzipereka pa utumiki wawo. Adutsa mwambiri koma izi ndi zazikulu zomwe mulungu watichitira powatsogolera mpaka lero pomwe atsimikiza kuti ali okonzeka kutumikira Mulungu, anatero sister Matchado. Polankhulapo mmodzi mwa asisteri omwe achita malumbiro awo a ku nthawi zonse sister terteza misomali athokoza mulungu powathandiza kukwaniritsa maloto awo. Si mphamvu kapena nzeru zathu koma timadalira chithandizo cha Mulungu kuti tifike pamenepa, anatero Sister Misomali. Chipani cha sacramentine kuno ku malawi chikupezeka mmadayosizi awiri mwa ma dayosizi 8 omwe alipo mdziko muno omwe ndi a Dedza ndi Mangochi. ",13 "Papa Yohane Paulo Wachiwiri Anali Wokonda Kupemphera, Wachilungamo Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wati Papa Yohane Paulo Wachiwiri Woyera anali munthu wokonda kupemphera komanso wokonda chilungamo. Papa Yohane Paulo Wachiwiri Woyera Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican Papa Francisco walankhula izi lolemba ku likulu la mpingo ku Vatican pa Misa yokumbukira kuti papita zaka 100 pamene Papa Yohane Paulo Wachiwiri anabadwa. Iye wati Papa Yohane Paulo Wachiwiri ngati mbusa, anali wokonda kukhala pafupi ndi anthu, wokonda kupemphera komanso wokonda chilungamo. Lolemba pa 18 May Papa Francisco watsogolera Misa yomwe yachitikira pa manda a Papa Yohane Paulo Wachiwiri Woyera. Iyi inali Misa ya padera yothokoza Mulungu chifukwa cha mphatso ya mtengo wa patali ku dziko la pansi ya Papa Yohane Paulo Wachiwiri. Pa Misayo Papa Francisco wati Papa Yohane Paulo Wachiwiri anali mbusa yemwe amakonda nthawi zonse kukhala pafupi ndi anthu, wokonda kupemphera komanso wokonda chilungamo. Mulungu amakondadi anthu ake. Mulungu anayendera anthu ake zaka 100 zapitazo kudzera mwa mwana yemwe anabadwa ku Poland. Anakula nakhala wansembe, episkopi mpaka kukhala Papa. Zoonadi Mulungu amakonda anthu ake ndipo amawayendera anthu akewo, watero Papa Francisco pa Misayo. Papa Francisco wati Papa Yohane Paulo Wachiwiri anali wokonda kupemphera chifukwa anadziwa kuti ntchito yoyamba ya episkopi ndi kupemphera. Papa Yohane Paulo Wachiwiri anali wokonda kukhala pafupi ndi anthu nchifukwa chake anayenda maulendo ambiri mmaiko osiyana-siyana kukalimbikitsa akhristu komanso kukasaka nkhosa zotayika ndipo iye watinso Papa Yohane Paulo Wachiwiri anali wokonda chilungamo kuonetsetsa kuti mmaiko muli mtendere komanso anali wa chifundo popeza chilungamo ndi chifundo zimayendera limodzi. Pomaliza Papa Francisco wati ngati lero anthu akukamba za chifundo cha Mulungu (Divine Mercy) ndi chifukwa cha Papa Yohane Paulo Wachiwiri. Papa Yohane Paulo Wachiwiri Woyera anabadwa pa 18 May, 1920 ku Poland. Iye anakhala Papa kwa zaka 27 kuyambira 1978 mpaka kumwalira kwake mchaka cha 2005. Ngati Papa anayenda maulendo 104 mmaiko osiyana-siyana kuphatikizapo dziko la Malawi mchaka cha 1989 kuyambira pa 4 mpaka 6 May. ",13 "HRDC Siyipepesa-Mtambo Nduna yazofalitsa nkhani a Mark Botomani anapempha speaker wa nyumba ya malamulo kuti ayitanitse ku nyumbayi wapampando wa bungwe la HRDC a Timothy Mtambo kuti akapepese pa mau omwe ati adalankhula lachiwiri pomwe amatuluka kunyumba-yi. Mtambo ndi Trapence pa tsiku lomwe analowa mnyumba ya malamulo A Mtambo akuti adauza atolankhani pomwe amatuluka ku nyumbayi kuti aphunguwa ndi achibwana mawu omwe ndunayi yati ndi osayenera. Pamenepa, a Botomani anati ndi koyenera kuti a Mtambo apite kunyumba-yi ku komiti yomwe a speaker angasankhe kuti iwo akapepese pa mauwa. Iwo amalankhula izi masana a lachitatu kunyumba ya malamulo pomwe nyumbayi imayamba zokambirana zake. Kwa ineyo ndikuona kuti mawu amenewa ndi achipongwe, polankhula kuti ifeyo ndi anthu azibwana komanso ndife ana amene ndi mawu oti sakuyenera kulankhulidwa ndi munthu aliyense kwa nzake, potengera kuti analankhulira kuno ku paliyamenti ndikupemphanso asipikala kuti asankhe komiti yoti a Mtambo akapepeseko pa chipongwe chomwe achitachi, anatero a Botomani. A Botomani ati nkhaniyi yafika kale kwa sipikalayu ndipo anaena kuti achitapo kanthu akakambirana bwinobwino koma iwo apempha asipikala wa kuti achite machawi powayitanitsa a Mtambo ku komiti yomwe asankheyi kuti azapepese poti chipongwechi chalankhulilidwa ndi kwa sipakala omwe anyumbayi. Koma polankhula ndi imodzi mwa wailesi zina mdziko muno wacbiwiri kwa mkulu wa bungwe la HRDC a Gift Trapence ati sangapepese ndipo aphungu a mbali ya bomawa ndi omwe akuyenera kupepesa powatchula iwo kuti ndi zigawenga. ",11 "CCJP Yadzudzula Mchitidwe wa Ziwawa pa Ndale Mdziko Muno Bungwe la chilungamo ndi mtendere la Catholic Commision for Justice and Peace (CCJP) lati ndi lokhudzidwa ndi mchitidwe wa ziwawa pa ndale umene ukuchitika mdziko muno pomwe anthu ali mkati mokonzekera chisankho chatsopano cha mtsogoleri wa dziko lino chomwe chidzachitike pa 2 July chaka chino. Wasayinira chikalatacho-Chibwana Bungweli lanena izi kudzera mu chikalata chake chomwe latulusa podzudzula mchitidwe-wu. Chikatatachi chati ndi zomvetsa chisoni kuti andale ena sakutenga nawo gawo pophunzitsa anthu owatsatira za kuipa kwa mchitidwe wa ziwawa zomwe zikuononga dziko lino. Bungweli lati mzika za dziko lino zikuyenera kuti ziwunike bwino andalewa pomwe akuyembekezeka kukaponya voti pa chisankho cha president wa dziko pa 2 July chaka chino. Mwazina chkalati chatsindika zina mwa ziwawa komanso zamtopola zomwe zachitika mmadera ena mdziko muno monga kuphwanyidwa kwa zipangizo za bungwe la MEC ku malo ochitira kalembera, kuwotchedwa kwa nyumba, komanso kuphedwa kwa anthu ena, zomwe anthu akuganizira kuti akuchita izi ndi a chipani cha Democratic Progressive (DPP). ",11 "NB Idandaula ndi Kugula Luso la ICT Lakunja Wolemba: Thokozani Chapola Banki ya National yalangiza makampani owona za chuma mdziko muno kuti aganizire kupereka mwayi kwa achinyamata a mdziko muno omwe ali ndi ukadaulo okhudza luso la makono ndi cholinga chowathandiza kukweza luso lawo komanso kutukula dziko lino. Wapempha kampani zizitenga anthu a luso la ICT a mdziko muno-Kawawa Mkulu wabanki ya National a Macfussy Kawawa ndi yemwe wanena izi lachinai mboma la Mangochi pa mkumano wa akadaulo a luso la makono la ICT omwe unachitikira ku Sunbird Nkopola kumenenso bankiyi inapereka mphotho kwa omwe achita zinthu za luso pa nkhani za ICT. A Kawawa anena izi potsatira dandaulo la anthu ena kuti kampani zambiri zoona za chuma mdziko muno zikumakonda kupereka mwayi kwa kampani za ICT zakunja kuposa za mdziko muno. Pamenepa a Kawawa alangiza achinyamata a luso la mtunduwu mdziko muno kuti adzigwira ntchito limodzi ndi cholinga choti luso lawo liwonekere patali kwa anthu omwe angathe kulifuna. Polankhulapo mtsogoleri wa bungwe la Information Communication Technology Association Of Malawi (ICTAM) a Bram Fudzulani ati ndi okondwa ndi mmene ntchito za ICT zikukulira mdziko muno koma wati akuyesetsa kuti awonetse poyera ntchito zomwe amagwira kuti makampani akonde kupereka mwayi kukampani za ICT za mdziko muno kusiyana ndi za kunja. ",2 "Alimbikitsa Makatekist Amvetse za Baibulo Makatikisti a mu dayosizi ya Mangochi awapempha kukhala zitsanzo zabwino powerenga komanso kuphunzitsa ena baibulo. Bambo Samuel Malamulo ndi omwe anena izi pa maphunzirowa omwe anachitikira ku St. Marys Pastoral Centre mu dinale ya Mpiri pa mutu woti Baibulo Ndi Nyale Ya Moyo Wanga. Iwo anatinso ma catechist azikhala ndi chidwi chowaphunzitsa akhristu ena ndipo akabwerera ku maparish kwawo akathandize ena kumvetsa baibulo. Iwowa ngati atsogoleri akuyenera kuti akachoka pano akathe kuphunzitsa akhristu ku madera kwawo zokhudza baibulo choncho akuyenera kumvetsa bwino cholinga cha maphunziro amenewa, anatero bambo Malamulo. Mmodzi mwa ma katekist omwe anachita nawo maphunziro-wa a Matthews Mchakulu ati maphunzirowa akawathandiza kuwaphunzitsa akhristu a mma PARISH mwawo kumvetsa baibulo. Maphunziro amenewa atithandiza kwambiri ndipo atithandiza kumvetsa bwino za baibulo. Tikabwelera ku parish kwathu tikatha kuphunzitsa bwino akhristu athu, anatero a Mchakulu. ",13 " Mafumu sanunkha kanthu pandale Kafukufuku amene achita akadaulo a zandale mdziko muno wasonyeza kuti ngakhale mafumu ena amayesetsa kusanthula momwe Amalawi akuganizira pandale, Amalawi salabadira zonena za mafumuzo. Mmodzi mwa akatswiriwo, Happy Kayuni amene amaphunzitsa ukadaulo pandale ku Chancellor College, adati zotsatira zimene adapeza adzazikhazikitsa pa 17 March ku Sunbird Mount Soche mumzinda wa Blantyre. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mafumu sayenera kuika mlomo pankhani za ndale Izi zikudza patangotha sabata kuchokera pamene anthu ena adakuwiza Paramount Lundu pamaliro a mfumu Kabudula ku Lilongwe pomwe mwa zina adati chipani cha MCP chidalamulira dziko lino zaka 31 ndipo sichidzalamulilanso kuchokera mu 1994 pomwe chidachoka mboma. Lundu adatinso chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) ndicho chidzalamulire mu 2019. Koma polankhula ndi Tamvani, Kayuni adati kafukufukuyo adapeza kuti mafumu amalemekezedwa ndi kukhulupiliridwa pankhani za miyambo yawo osati popanga ganizo la ndale. Tikatulutsa zotsatirazo, anthu adzadzionera okha kuti anthu amalemekeza ndi kukhulupilira mafumu pankhani za chikhalidwe chawo koma alibe chikoka pakapangidwe ka ganizo la munthu amene asankhe pa ndale, adatero Kayuni. Kayuni adakana kutambasula bwino kuti kafukufukuyu adamuchita nthawi yaitali bwanji, ndi anthu angati, njira yomwe adatsata pofunsa mafunso komanso mafunso amene amafunsidwa. Iye adati zonse adzazitambasula bwino akamukhazikitsa. Iye wati chanzeru chomwe mafumu angachite nkuphathirira ku udindo wawo ndi kumalimbikira ntchito yawo mmalo motaya nthawi ndi zandale powopa kutsukuluza ulemu omwe ali nawo. Pa zomwe mafumu ena akhala akunena kuti amayenera kukhala mbali yaboma, Kayuni wati ichi nchilungamo chokhachokha koma waunikira kuti mpofunika kutanthauzira bomalo molondola. Mpofunika kutanthauzira bwinobwino liwu lakuti boma chifukwa mwina mafumu oterowo amaona ngati boma nchipani cholamula pomwe si choncho. Boma limagawidwa patatu: Mtsogoleri ndi nduna zake, aphungu a Nyumba ya Malamulo komanso mabwalo oyendetsa. Akamati amakhala mbali ya boma, sakulakwa koma aziganizira tanthauzoli kuti iwo ngopanda mbali ndipo ntchito yawo nkutsogolera anthu awo pankhani zamakhalidwe ndi chitukuko. Ndale nza anthu ena, adatero Kayuni. Polankhula ku maliro a T/A Kabudula, Senior Chief Lundu adaweruziratu kuti chipani cha DPP ndicho chidzapambane pachisankho cha 2019 ndipo kuti kaya wina afune kaya asafune, mafumu ena mdziko muno sadzaleka kusapota mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika ndi chipani cha DPP. Ngati tili pansi pa ulamuliro wa Mutharika ndi chipani cha DPP, chotiletsa kumusapota nchiyani? Choti mudziwe nchakuti chipani cha DPP chikuyenera kulamula mpaka 2019 ndipo chidzapitiliza kuchoka apo, adatero Lundu kumaliroko. Iye adapitiriza kunena kuti chipani cha Malawi Congress Party (MCP) chomwe mtsogoleri wake Lazarus Chakwera adali pa maliro pomwepo chisamalote zodzalamuliranso ndipo kuti kwake kudatha momwe chidatuluka mboma ngati chipani cholamula. Chakwera atafunsidwa ndemanga yake ndi Tamvani pa nkhaniyi adati alibe mau aliwonse kenako nkuseka. Oyendetsa nkhani za mafumu ku unduna wa Maboma angonoangono Lawrence Makonokaya adati timutumizire mafunso omwe tikuyembekezera mayankho ake. Zotsalira Tikuchezanso ndi kadaulo wina amene adacchita nawonso kafukufukuyo. ",8 "Boma Lilimbana ndi Mchitidwe Odzembetsa Anthu Wolemba: Sylvester Kasitomu Unduna owona za chitetezo cha mdziko wati uyesetsa pa ntchito yolimbana ndi mchitidwe ozembesta anthu (Human Trafficking) umenenso wakula kwambiri mdziko muno. Nduna mu undunawu a Nicholas Dausi anena izi mu mzinda wa Lilongwe pa mwambo wokumbukira tsiku lolimbana ndi mchitidwe wozembetsa anthu pa dziko lonse. A Dausi ati ndizomvetsa chisoni kuti mchitidwe-wu ukuchitikira aliyense ngakhale anthu ophunzira kumene zomwe zikuyika pachiopsezo miyoyo ya anthu ambiri choncho ati unduna wawo ugwirana manja ndi magulu onse okhudzidwa polimbana ndi mchitidwewu. Zomatenga anthu kuti tili ndi ntchito zoti mukagwoire mmaiko wena pamapeto pake ndikumakawagwiritsa ntchito za uhule ndi zina tikudzidziwa ndipo tikufuna kuti zitheretu mdziko muno, anatero a Dausi. Ndipo polankhulapo mkulu oyanganira nkhani zozembetsa anthu ku nthambi ya bungwe la united nations yoona nkhani zokhudza makhwala ozunguza ubongo mdziko muno a Maxwel Matewere anati nthambi zonse zoona za malamulo mdziko muno ziwunika nkhaniyi kuti itheretu ndipo anthu omwe apezeke akhudzidwe ndi mchitidwewu kuti amangidwe. Anthu ena amangidwa kale pokhudzidwa ndi milanduyi ndipo ena anchajidwa kale ndipo ine ndi osangala kuti boma latengapo gawo pofuna kuteteza anthuwa, anatero a Matewere. Anthu amangidwa pokhudzidwa ndi milanduyi ndi okwana 32 ndipo mwa anthuwa 16 ndi omwe milandu yawo inatha ndipo akugwira ukaidi kundende za mdziko lino. ",14 " Voti yotengera zigawo ilipobe Amalawi akadali ndi mtima wovota potengera chigawo chomwe amachokera ndi munthu kapena chipani chomwe akulumikizana nacho mnjira inayake makamaka mtundu. Mwachitsanzo, pa zisankho ziwiri zapitazi za 2014 ndi 2019, chipani cha DPP chakhala chikupeza ma voti ambiri ku mmwera, MCP mchigawo chapakati pomwe kumpoto kudavotera kwambiri zipani za UTM and PP. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Duwa: Anthu ali kale ndi mbale Zotsatira za chisankho cha chaka chino zawonetsa kuti kavotedwe ka anthu sikadasinthe kwenikweni ndipo zangokhala ngati mkopera wa zotsatira za chisankho cha 2014 makamaka kwa zipani za MCP ndi DPP zomwe zimapikisana kwambiri. Mkulu wa mgwirizano wa mabungwe okhudzidwa ndi zisankho la Malawi Electoral Support Network (Mesn) Steve Duwa wati izi zili choncho chifukwa anthu saphunzitsidwa mokwanira za momwe angasankhire atsogoleri komanso zipani za ndale zimalephera kutambasula mfundo zake kuti anthu asinthe maganizo pambali yovotera. Anthu ali kale ndi mbali potengera zigawo zochokera chifukwa aliyense amafuna kukokera kwake koma malingaliro oterewa akhonza kusintha potengera momwe anthu aphunzitsidwira pa kasankhidwe ka atsogoleri komanso momwe zipani zatambasulira mfundo zake, adatero Duwa. Katswiri pa ndale Ernest Thindwa adati kuvota kwa malingaliro otere kawirikawiri kumachititsa kuti mtsogoleri azisankhidwa ndi anthu ochepa zomwe ngakhale zimaloledwa mdziko muno potengera malamulo achisankho, nzosayenera mu demokalase. Demokalase imatanthauza kuti anthu azisankha mtsogoleri yemwe akufuna ndipo azisankhidwa ndi anthu ambiri. Mwachidule, opitirira theka la anthu onse omwe adaponya voti ndiye kuti demokalase ikuyenda, adatero Thindwa. ",11 " Dz Young Soccer, Mighty adutsa Chikho cha Standard Bank chayamba ndi moto pamene matimu a asirikali a Kamuzu Barracks ndi Mafco FC aona msana wa njira atakwapulidwa ndi Dedza Young Soccer FC komanso Be Forward Wanderers kudzera mmapenote. Chikho cha K10 miliyonichi chidayamba modabwitsa Lachitatu pamene timu ya Kamuzu Barracks idaona mdima pa Civo Stadium itachitidwa chiwembu ndi Dedza Young Soccer kudzera mmapenote. Masewerowo adathera 2-2 ndipo nthawi ya mapenote Young Soccer idalimba chifu pokakamizabe asirikaliwa kuti atuluke mchikhochi. 10 kwa 9 ndi momwe mapenotewo adathera, kukomera anyamata a ku Dedza. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Lachinayi udalipoliponso pabwaloli Wanderers kulimbana ndi asirikali a Mafco. Masewerowanso adatheranso mmapenote atalepherana duu kwa duu ndipo Wanderers idapuntha Mafco 4-3 mmapenotewo. Mafco idali ndi mwawi wambiri moti ikadatha kuchinya zigoli mphindi 90 koma zonse zidangothera hiii! Iyitu idali ndime yachipulula ndipo matimu amene achita bwinowa alowa mndime ya makotafainolo. Apa ndiye kuti Dedza iphana ndi Civo mndimeyi pamene Wanderers ikumana ndi Red Lions. Mmakotafainolo ena, timu yomwe ikuteteza chikhochi, Silver Strikers, ikwapulana ndi Blue Eagles pamene Moyale Barracks ikumana ndi Big Bullets. Kochi wa Wanderers Elia Kananji adati ali ndi chiyembekezo kuti timu yake ichita zakupsa mchikhochi. Adali masewero ovuta koma Mulungu adali mbali yathu. Tikukhulupirira kuti Mulungu yemweyo akhala nafe mumpikisanowu mpaka kumapeto, adatero Kananji. Naye Pofera Jegwe, kochi wa Dedza Young Soccer, adati kupambana kwawo ndi chithokozo kwa masapota awo. Mukudziwa kuti tidachita kuvoteredwa kuti tisewere mchikhochi, ndiye kupambanaku ndi njira imodzi yothokoza amene adativoterawo, adatero Jegwe. Bungwe la FAM lomwe likuyendetsa mpikisanowu litulutsa masiku amene makotafainolowa aseweredwe. ",16 " Minibasi zikwera Mwachinunu Nthawi zonse minibasi zikamakweza mtengo, makamaka mafuta akakwera, bungwe la eni minibasi limalengeza, ndi kuika mitengo ya minibasi kuti aliyense adziwe. Koma kuchokera Loweruka lapitalo, mitengo ya minibasi mmadera ena idakwera mwachinunu. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Izi zidachitika patangotha tsiku limodzi kuchokera pomwe oyendetsa minibasi adanyanyala ntchito zawo ati pokwiya ndi zilango zina zimene amalandira akaphwanya malamulo a pamsewu. Amalawi amene tacheza nawo ku Blantyre, Lilongwe ndi Mzuzu adati ndiokhudzidwa ndi kukwezaku, komwe cholinga chake sichikumveka. Mandiya: Okwera akuyenera kupereka yochuluka basi Mmodzi mwa anthu omwe akhudzidwa ndi mitengoyi, Sydney Chingamba wa ku Chilomoni yemwe amagwira ntchito ku Ginnery Corner mumzinda wa Blantyre, wati ichi ndi chitonzo ndipo okwera akuyenera kuchitapo kanthu kuti mitengo ibwerere. Kafukufuku wa Msangulutso wapeza kuti mitengoyi yakwera ndi K50 kapena K100 mmadera osiyanasiyana mmizindayo. Malingana ndi mmodzi mwa madalaivalawa mu Limbe, Fatchi Madani, iyi ndi njira yoti galimoto itulutse ndalama zomwe eni minibasi amafuna patsiku ngakhale pali malamulo okhwimawa. Okwera akuyenera kupereka ndalama yochuluka basi. Patsiku bwana amafuna K10 000 ndipo kutenga atatu pampando pa K500 kukawasiya kwa Goliati ndi phada ameneyo. Ngakhale tisatenge anayi-anayi pampando ndalama izipezeka yokwanira chifukwa cha mitengoyi, adatero Madani. Naye Phillip Bwanali, woyendetsa galimoto pakati pa Limbe ndi Blantyre, adati akweza mitengo chifukwa sakuloledwa kunyamula katundu [chimanga, mtedza ndi zina] yemwe okwera amamulipira mwa padera. Tatero kuti tisavutike ndi kupewa ena kuyamba kuba ndi umbanda. Mmene chilili chuma cha dziko lino anthu ambiri sangakwanitse kutenga katundu pa matola omwe ndi okwera mtengo kusiyana ndi maminibasi, iye adatero. Poyankhapo, mkulu wa bungwe la eni minibasi la Minibus Owners Association of Malawi (Moam), Coaxley Kamange adati ndi odabwa ndi zimenezi ndipo wangomva mphekesera kuti madalaivala achita moteremu. Izi sizikutikhudza. Aliyense akhoza kuchita chili chonse ndi mitengo chifukwa lamulo likulola anthu kutero. Takhala tikudzudzulidwa ndi bungwe la Competition and Fair Trading Commission (CFTC) pamene timakonza mitengo mmbuyomu ndipo tidasiya, adatero Kamange. Iye adati izi ndi zosokoneza anthu chifukwa akudziwa zakusinthaku ali mminibasi kapena padepoti. Timayenera kutenga gawo pa chiganizochi kuphatikizapo okwera kuti mitengo ikhale yokomera onse. Bungweli [CFTC] lidati tisamakonze mitengo ya minibasi, koma padakalipano ndondomeko yabwino palibe, adatero Kamange. Mkulu wa bungwe loona ufulu wa okwera la Passengers Welfare Association of Malawi (Pawa), Don Napuwa, adati izi ndi zokhumudwitsa ndipo madalaivala sakuyenera kukweza mitengo ya galimoto chifukwa boma langokhwimitsa ndi kuyamba kutsatsa malamulo omwe adalipo kale. Madalaivala akusokoneza. Ngakhale kunyanyala ntchito komwe adachita sabata yatha eni galimoto sadadziwitsidwe. Mitengoyi imakwera potengera mtengo wa mafuta ndipo mafuta sanakwere. Oyendetsawa alibe danga lokweza mitengo, adatero Napuwa. ",15 " Katsoka: Mtsogoleri wa alakatuli Ulakatuli ndi limodzi mwa maluso omwe akuphukira kumene mdziko muno. Zaka zambiri zapitazo, anthu samatenga ndakatulo ngati njira yofalitsira uthenga kapena kuphunzitsa monga momwe zikukhalira pano. Pazaka zochepa zokha, alakatuli mdziko muno atumphuka ndipo anthu ambiri ayamba kukonda ndakatulo. Alakatuliwa adakhazikitsa bungwe lawo lomwe mtsogoleri wake ndi Felix Njonjonjo Katsoka. STEVEN PEMBAMOYO adacheza naye motere: Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Katsoka ndi mlakatuli wodziwa kuluka mawu Tandiuza dzina lako ndi komwe umachokera. Ine ndine Felix Njonjonjo Katsoka. Ndimachokera mmudzi mwa Chingamba mboma la Ntcheu koma pano ndikukhala ku Nkhotakota. Ndidaphunzira za uphunzitsi koma ndimagwira ntchito ya zaumoyo kumbali ya zakudya zamagulu. Utsogoleri wa alakatuli udaulowa liti? Ndidauyamba mchaka cha 2009. Malingana ndi malamulo athu, timayenera kukhala ndi zisankho zaka zisanu (5) zilizonse moti panopa tili kalikiriki kuthamangathamanga kuti tipeze ndalama zopangitsira nkhumano ina komwe tidzakhalenso ndi zisankho. Kodi bungwe limeneli lidayamba liti? Bungweli lidayamba mchaka cha 1997 pomwe alakatuli adakumana kubwalo la masewero la Kamuzu Stadium. Ena mwa akatakwe omwe adali kumeneko ndi monga Laurent Namarakha, malemu Aubrey Nazombe, Edward Chitseko ndi malemu George Chiingeni. Pa 4 September, 1998, bungweli lidalembetsedwa kunthambi ya kalembera wa mabungwe. Cholinga chake nchiya? Cholinga cha bungweli ndi kufuna kutukula luso la ulakatuli mMalawi muno komanso kufuna kufalitsa mauthenga ndi kuphunzitsa anthu kudzera mndakatulo monga momwe amachitira azisudzo kapena oyimba. Kodi munthu amafunika chiyani kuti akhale mlakatuli? Choyambirira ndi kudzipereka kukhala ndi mtima ofunitsitsa kukhala mlakatuli. Sizilira kupita kusukulu, ayi, ndi luso ndithu lachibadwa. Ine sindidaphunzireko ndakatulo komanso alakatuli ambiri omwe ndimadziwa sadachite maphunziro a ndakatulo, ayi.katsoka Nanga ndakatulo yabwino imafunika kukhala ndi chiyani? Ndakatulo yabwino imayenera kukhala ndi phunziro, msangulutso komanso izigwirizana ndi zachikhalidwe kapena nkhani yomwe ikunenedwa. Mundakatulo muli ufulu wosankha mmene ukufunira kuti mavume azimvekera. Palibe malamulo akuti ndakatulo izimveka motere, ayi. Kwathu kuno, ndakatulo zambiri zimakhala zokhudza chikhalidwe cha Chimalawi, makamaka potengera chiphunzitso ndi malangizo. ",0 " Chikondi chidayambira kuubwana Akuti chikondi chidayambira kuumwana kalelo pomwe ankasewerera limodzi nkumakula pa Kalera ku Salima ndipo lero akhala thupi limodzi. Francis Tayanjah-Phiri, mtolankhani wodziwika bwino yemwe akugwira ntchito kukampani ya Times Group, sabata yathayi adamanga chinkhoswe ndi nthiti yake, Stella Kamndaya, yemwe ndi mphunzitsi ku Lumbadzi mboma la Dowa. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Tayanjah ndi dona wake Stella kugonekerana khosi patsiku la chinkhoswe Tayanjah adati mzaka za mma 1980 mayi ake ankaphunzitsa pasukulu ya pulayimale ya Kalera limodzi ndi bambo ake a Stella ndipo mabanja awiriwa adali pachinzake cha ponda-apa-nane-mpondepo, zomwe zidabzala mbewu ya chikondi mwa ana awo. Pa anzanga onse yemwe ndinkagwirizana naye kwambiri adali iyeyu kufikira pomwe ndidapita kukapanga maphunziro a utolankhani ndipo naye adakapanga kozi ya uphunzitsi. Kuyambira pamenepo tinkangomva kuti wina ali uku ndipo wina ali uku, adatero Tayanjah. Iye adati kutalikiranako sikudafufute chikondi chomwe adali nacho pakati pa wina ndi mnzake ndipo ankaganiziranabe nthawi zonse mpakana mwamwayi adakumana aliyense akuyendera zake mumzinda wa Lilongwe, nkukumbukira kale lawo. Chifukwa cha chikumbumtima cha kale lathu, titakumana padalibe chilendo chilichonse ndipo tidayambiranso kucheza, koma ndidaona kuti ubale womwe adatiphunzitsa makolo athu kalelo tiuonetsere kudziko, adatero Tayanjah. Iye adati nyengo ikupita ndi machezawo adapereka maganizo a banja ndipo mtima wake udadzadza ndi chimwemwe choopsa Stella atavomera. Naye Stella adati kwa iye adali ngati maloto okoma oti ukadzuka zomwe umalotazo zikuchitikadi uli maso. Ndidalibe chifukwa chotengera nthawi kuti ndikaganize kapena kuti ndimuone kaye chifukwa ndakula naye ndipo nzeru zake, khalidwe lake, chikondi chake zonse ndidali ndikudziwa kale kuchokera tili ana, adatero Stella. Iye adati ali ndi chiyembekezo cha banja lapamwamba ndi Tayanjah ndipo pemphero lake ndi lakuti Mulungu awapatse luntha lomwe adapatsa makolo awo pakasungidwe ka banja ndi kaleredwe ka ana. Tayanjah amachokera mmudzi mwa Rubeni, T/A Kambwiri ku Salima ndipo Stella kwawo ndi kwa Daniel, T/A Maganga ku Salima komweko. ",15 " ankawerenga nkhani pa mij Ndi mawu okha, MarcFarlane Mbewe wa Capital Radio adachiritsidwa. Awa ndi makumanidwe a mnyamatayu ndi Lisa Lamya, mtolankhani wa Yoneco FM (YFM). Nkhaniyi idayamba mu 2014, apo nkuti Lisa akugwira ntchito ku MIJ FM. Kumeneko, namwaliyu ankawerenga nkhani. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Lero ali ndi mwana mmodzi, Evan: Macfarlen ndi Lisa Ena mwina amangomva namwaliyo akamawerenga nkhani, koma kwa MarcFarlane, zimamupatsa uthenga wina. Mawu ake ozuna komanso Chingerezi chake chothyakuka zidanditenga mtima, adatero MarcFarlane. Ndidafunitsitsa nditapalana naye ubwenzi. Mwachangu ndidamusaka pa Facebook. Ndidamutumizira pempho kuti akhale mnzanga. Macheza akuti adayamba. Koma mnyamatayo atapempha nambala, Lisa adamukaniza. Ndidaponya mfundo ndipo mapeto ake adandipatsa nambalayo, adatero. Apo zidayamba kusongola ndipo mathero ake kudali kukumana pamene mfundo zenizeni zidaumbidwa. Lero Lisa akubwekera posankha mnyamatayu. MarcFarlane ndidamukonda chifukwa ndi ndi wanthabwala zedi koposa zonse amakonda kupemphera, idatero njoleyo. Pamene MarcFarlane akuti: Lisa ndi mkazi wokoma mmaso komanso wakhalidwe. Awiriwa ali ndi mwana wa miyezi isanu dzina lake Evan. Ukwati akuti apangitsa chaka chikudzachi koma chinkhoswe ndiye chidali pa 5 March 2017. MarcFarlane, woyamba mwa ana atatu ndi wa kwa Chimaliro mboma la Thyolo. Lisa, woyamba mwa ana awiri ndi wa kwa Ben Chauya ku Ntcheu. ",15 "Ndimamupitirira Wawa gogo, Ndili ndi zaka 17 ndi[po pali mnyamata wina wa zaka 20 yemwe akundifuna. Ndimamukonda koma vuto ndi lakuti iyeyo ndi wamfupi kuposa ine. Ndimachita manyazi ndikamayenda naye. Ndimulole? C Zikomo C, Sindikuonapo vuto loti musamulolele! Kutalika kukhale nkhani? Chikondi chimachoka mumtima ndipo sichiyenera kuona ngati wina ndi wamtali kapena wamfupi, woonda kapena wonenepa, woona kapena wosaona ndi zina zotero. Chabwino nchiyani kuti mudzapeze mnyamata wamtali ngati inu kapena kukuposani koma alibe chikondi kapena kukhala ndi mwamuna ameneyu yemwe amakukondani nanunso kumukonda. Muloleni ameneyo basi. ",12 "Apolisi Akusasaka Opha Mkazi Wake Wakale Wolemba: Sylvester Kasitomu ntent/uploads/2019/09/chigalu.jpg"" alt="""" width=""397"" height=""264"" />Chigalu: mayiyo amakana kuti abwelerane Apolisi ku Ntcheu akusakasaka mkulu wina amene wapha yemwe anali mkazi wake kaamba kokana kuti abwelerane pa ubwenzi. Mneneri wa apolisi mbomalo Hastings Chigalu wati mamunayo ndi Ndaipa Odala ndipo mayiyo ndi Idesi Lyson wa zaka 19. Chigalu wati awiriwa anali pa ubwenzi ndipo anapatsana pathupi koma mamunayo anakana kuti mimbayo siyake. Kwa nthawi yonseyi mayiwa akhala akuvutika okha ndi mwanayi kufikia sabata latha pomwe bamboyu anayamba kuzachonderera kuti abwerere pa banja ndi malemuwa. Malemuwa atakana zobwerera pa banja ndi oganiziridwawa zinawakwiyitsa ndipo anaganiza zowadikirira panjira pomwe malemuwa amyenda mu nsewu wina ndikuwabaya ndipo anafera pamalo amwewo, anatero Chigalu. Malipoti akuchipatala atsimikiza za imfayi ndipo ati mayiyu wafa kaamba kotaya magazi ambiri. ",7 " Ndi Walter, Mijiga Kapena Yabwanya? Atatsatsa mfundo zawo masiku apitawa, omwe akulimbirana maudindo kubungwe loyendetsa masewero a mpira wa miyendo la Football Association of Malawi (FAM) akhala akukumana maso ndi maso pazisankho zomwe zikuchitika lero. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Nthumwi zokwana 36 zochokera kunthambi za FAM ndi zomwe zitaponye voti pamsonkhano waukulu womwe ukuchitikira mboma la Mangochi. Akuimanso: Nyamilandu Omwe akupikisana paudindo wa pulezidenti ndi yemwe pakalipano ali pampandowu, Walter Nyamilandu, Wilkins Mijiga komanso a Willy Yabwanya Phiri. Akuluakuluwa sabata yathayi adali kalikiriki kupereka mfundo zawo pazomwe akufuna adzachite akasankhidwa paudindowu. Polankhula mumzinda wa Lilongwe, Nyamilandu adalonjeza kuti akapambananso adzakhazikitsa ndondomeko zoonesetsa kuti mpira wa mmakwalala ukupita patsogolo komanso kuti mpira ukubweretsa ndalama zochuluka maka mmakalabu osiyanasiyana. Wakonzeka: Mijiga Kumbali yake Yabwanya adalonjeza kuti adzasula aphunzitsi a mpira ambiri omwe azitha kuphunzitsa anyamata achisodzera ndi cholinga choti luso lawo lipite patsogolo. Naye Mijiga pomema anthu kuti amusankhe, adati adzakhazikitsa njira zopezera ndalama ndi cholinga choti osewera, oyimbira komanso oyendetsa mpira azilandira ndalama zambiri. Pakalipano zikuonetsa kuti Nyamilandu atha kutenganso mpandowu kaamba koti mwa nthambi zisanu ndi zinayi za bungwe la FAM, zisanu ndi ziwiri zidalengezetsa kuti zili pambuyo pake. Ali momo: Yabwanya Phiri: Nthambi imodzi yokha ya Super League of Malawi ndi yomwe ikuti ili pambuyo pa Mijiga pomwe ya National Referees Committee ndi yomwe ikuti ili pambuyo pa Yabwanya. Koma zioneka komweko chifukwa voti ikhala yachinsinsi. Omwe akupikisana pampando wa wachiwiri kwa pulezidenti ndi Tiya Somba-Banda ndi James Mwenda. Mpikisano pampando wa wachiwiri kwa wachiwiri kwa pulezidenti uli pakati pa Pikao Ngalamila ndi Othaniel Hara. ",16 "Papa Wati Atsogoleri Athandize Anthu Awo Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Fransisco wapempha atsogoleri a mayiko kuti ayike ndondomeko zabwino zothandiza anthu awo. Papa Francisko Papa Francisco walankhula izi lolemba pa misa yomwe anatsogolera ku likulu la mpingo ku Vatican. Iye wati atsogoleri a mayiko ndi onse ochita ndale akuyenera kumachita zinthu zokhazo zomwe zingathandize pa ntchito zotetedza komanso kutukula anthu awo osati kuchita zinthu zongokomera iwo eni ndi zipani zawo. ",14 "Lutepo wakundende Bwalo lalikulu la milandu ku Zomba (High Court) Lachisanu lapitali lalamula Auswald Lutepo, yemwe ndi mmodzi mwa anthu omwe akuyankha milandu yokhudza kusolola ndalama za boma wotchedwa kuti Cashgate, kuti akakhale mndende kwa zaka 11 popezeka wolakwa pamlanduwu. Popereka chilango, jaji Redson Kapindu adati pamlandu woyamba wopanga upo pofuna kubera boma, Lutepo akaseweze zaka zitatu ndipo wachiwiri, wosolola ndalama zokwana K4.2 biliyoni, akaseweze zaka 8. Zilango zonsezi ziyendera limodzi kuyambira pa 11 June pomwe iye adapezeka wolakwa pamilandu yonse iwiri. Jajiyu adati wamumverako chisoni pamplandu wachiwiri kaamba koti adabwezako ndalama zokwana K370 miliyoni. ",11 " Sitalaka yatha, yaika amalawi pamoto Pomwe ogwira ntchito mboma ali pa sitalaka kufuna kuti malipiro awo akwere ndi K67 pa K100 iliyonse, anthu omwe amafuna thandizo la ogwira ntchito mbomawa tsopano ndiwo ali pamavuto adzaoneni. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Pomwe limafika Lachitatu nkuti maofesi ambiri aboma ali otseka. Kuchipatala kokha ndiko kudali kosatseka. Anamwino amene adakumana ndi mtsogoleri wa dziko lino Lolemba adati ngati madandaulo awo, kuphatikiza kukwezedwa kwa malipiro awo, sakwaniritsidwa pofika pa 26 February, nawonso achita sitalaka. Wophunzira wina pasukulu ya sekondale ya Nyambadwe adati kumeneko aphunzitsi a pulaimale ndi sekondale adayamba kunyanyala Lachiwiri sabata yatha. Mnyamatayu, yemwe ali fomu 3 ndipo ali ndi zaka 24, amagwira ntchito ya mnyumba ku Mbayani ndipo amalandira K5 000 pamwezi. Pandalamapo amachotsapo K4 700 kuti alipirire sukuluyo pateremu. Ndidachoka kwathu ku Mangochi chifukwa bambo anga adamwalira ndipo mayi anga ndiwo ankandilipirira sukulu. Iwo ankagulitsa tiyi. Koma zitawasokonekera, kusukulu adandithamangitsa. Nditapata ntchitoyi ndipomwe ndabwerera kusukulu. Ndimalimbikira kuti ntchitoyo ilipo ndikhale ndamaliza sukulu. Kunyanyala kwa aphunzitsi kukundiwawa chifukwa ntchitoyi mwina itha kutha zomwe zidzandivute kuti ndibwererenso kusukulu posowa ndalama, adadandaula mnyamatayu. Wophunzira wina yemwe ali sitandade 8 pa sukulu ya pulaimale ya Mbayani wati boma liwaganizire chifukwa mayeso ayamba posachedwapa. Sitidaphunzire mokwana, ndipo kwangotsala miyezi itatu kuti tilembe mayeso. Boma litiganizire zimenezi, adatero msungwanayo. Ndipo mnyamata wina pasukulu ya Nkolokoti ndipo ali sitandade 7 wati mayeso a aphunzitsi ayamba sabata ya mawayi kotero boma liwaganizire. Omwe akuchititsa izi adaphunzira kale ndipo ana awo ali msukulu za pulaiveti ndiye iyi si nkhani kwa iwo. Chonde boma liganizire, adatero mnyamata wa zaka 11. Mphunzitsi wina pa Mbayani adati mwana sakuyenera asemphe kanthu pano chifukwa mayeso ali pafupi. Chitsanzo a 8 ali ndi miyezi itatu yokha pomwe silabasi sadamalize, nanenso ndine kholo zikundimvetsa chisoni koma nanga nditani, adatero mphunzitsiyo. Ndipo Lachitatu, ana a sukulu zina mumzinda wa Blantyre adapita kusukulu ya Joyce Banda Foundation, yomwe ndi ya mtsogoleri wa dziko lino. Anawo adati akasokoneze maphunziro ati chifukwa ana kusukuluyo amaphunzirabe. Nawo maofesi a Road Traffic Lachitatu adali kotseka. Mkulu wina yemwe tidamupeza ku ofesiyi ndipo amafuna thandizo adati zamukhudza. COF ya galimotoyi yatha dzulo pa 19, ngati ndingayendebe pamsewu ndiye kuti andigwira. Akangondigwira ndiyenera kulipira K3 500. Ndachita changu kudzakonzetsa koma apa pali potseka. Boma lidziwe kuti omwe tikuvutika ndife osati iwo, adatero mkuluyo. Koma mkulu wa bungwe la ogwira ntchito mboma la Civil Service Trade Union Eliah Kamphinda wati anthu omwe akuvutikawa akuyenera kufunsa omwe achititsa kuti mavutowa adze. Pali ena achititsa izi, afunse azamaphunziro omwe adzetsa zonsezi, adatero Kamphinda. Iye adati ku Lilongwe apereka kalata yachidandaulo ndipo kuyambira Lachinayi amayembekezeka kumakumana malo amodzi mpaka boma litayankha. Nduna ya zachuma Dr Ken Lipenga Lachiwiri lomwelo adati sizingatheke kuti boma likweze malipiro a ogqira ntchito mboma chifukwa kuti boma litero, ndiye kuti ndalama zimene boma limalipira a ntchito ake zidzakwera kuchoka pa K92 biliyoni kufika pa K276 biliyoni chaka chilichonse. Iye adanena izi pamsonkhano wa atolankhani omwe adaitanitsa a bungwe la International Monetary Fund (IMF). Izi zingatanthauze kuti ndalama za boma zonse zithera kulipira ogwira ntchito mboma. Mankhwala mzipatala tidzagulira chiyani? adazizwa Lipenga. Mkulu wa IMF kuno ku Malawi Tsidi Tsikata adati adapempha boma la Malawi kuti lichepetse ndalama zomwe limagwiritsa ntchito. Boma likuyenera kuonetsetsa kuti likugwiritsa bwino ntchito ndalama zomwe zilipo. Mmalo motaya nthawi ndi zazingono, bwenzi boma likuikapo mtima pogwiritsa ntchito bwino ndalamazo, adatero Tsikata. ",11 " Blessings Cheleuka wa pa JOY FM Amalawi ambiri kuyamba Lolemba mpaka Lachisanu nthawi ya 2 koloko kufika 4 koloko masana amatsegula wailesi ya Joy FM kuti amvere nyimbo zothyakuka zoimbidwa ndi Amalawi anzawo. Namandwa wophulitsa nyimbo zimenezi ndi Blessings Cheleuka, yemweso wachitapo mbali yaikulu kutukula alakatuli mdziko muno. STEVEN PEMBAMOYO adacheza naye motere: Cheleuka: Chilichonse nchotheka pamoyo wa munthu Dzifotokoze mkulu wanga. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ine ndine Blessings Cheleuka, ndimachokera mmudzi mwa Mothiwa kwa T/A Likoswe mboma la Chiradzulu. Ndine muulutsi wa pawayilesi komanso ndimakonda ndakatulo kwambiri. Ntchito yakoyi udayamba liti? Ndakhala ndikugwira ntchitoyi kwa zaka 12 ndipo ndagwira mnthambi zosiyanasiyana monga wolemba nkhani, mkonzi, muulutsi ndi zina. China choti mungadziwe nchakuti ndagwirako ntchitoyi kunyuzipepala ndi kuwayilesi komwe ndiye ndili ndi ukadaulo kwambiri. Akadaulo ambiri amakhala ndi komwe adaphunzirira ntchito, iwe udaphunzirira kuti? Choyamba, ndidaphunzira zautolankhani kusukulu yaukachenjede ya Polytechnic, nthambi imodzi ya University of Malawi. Kumeneku ndidaphunzira zomwe zimatenga kuti munthu ukhale mtolankhani mbali zonse. Kuchoka apo mmalo momwe ndakhala ndi kugwira ntchito monga Power 101 FM komwe ndidayambira ntchito; ndidaphunzirako za kuulutsa mapologalamu osanjenjemera chifukwatu kunena zoona ndi luso lapadera limenelija. Ndimayamikaso Mulungu ponditsogolera ndi kundiunikira. Nanga umaulutsa mapologalamu anji pawailesi? Ndimaulutsa mapologalamu ambiri monga Dimba Music yomwe imauluka kuyambira Lolemba mpaka Lachisanu nthawi ya 2 koloko masana mpaka 4 koloko madzulo; Zina Ukamva yomwe imauluka 8 koloko madzulo Loweluka; pologalamu ya ndakatulo yotchedwa Patsinde yomwe imayamba 8 koloko mmawa mpaka 10 koloko; Mfuwu Wa Chimwemwe kuyamba 6 koloko mpaka 9 koloko mmawa Lamulungu; ndi Gospel Top 20 ya nyimbo za uzimu komanso ndine ndimayanganira za uwulutsi kuwailesi ndi kanema za Joy. Ukutinso uli ndi chidwi pa zaulakatuli, umatengapo gawo lanji? Ndapanga zambiri monga kudzera mu pologalamu yanga ya Patsinde. Ndimafukula alakatuli omwe sadayambe kudziwika. Ndimakonzaso zochitika za alakatuli ndipo anthu ambiri amazikonda. Ukafatsa umakonda kutani? Ndimakonda kuonerera mapologalamu a pakanema ndi zauzimu basi. Mwina okutsata amangoti ndiwe muulutsi, ungawauzenji za iwe? Ine ndine Blessings Cheleuka odziwika kuti Bule wanu pazausangalatsi ndipo cholinga changa nkusangalatsa Amalawi basi. ",9 " Tinkapita kumpira wa Silver Ena akangomva za masewero ampira amalingalira zogenda, kuvala ziyangoyango kapena kuimba nyimbo basi komatu monga zochitika zina zilizonse, iyi ndi nthawi yokumana ndi anthu osiyanasiyana okonda zinthu ndi zochita zosiyanasiyananso. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Onse amakonda timu ya Silver: Daniel Kudzera mumtendere woterewu, ena amachita mwayi waukulu pamoyo wawo mwina mpaka kupeza nthiti yawo monga momwe zidakhalira ndi Daniel Nthala wa mmudzi mwa Yesaya, kwa mfumu yaikulu Kalumbu ku Kamphata mboma la Lilongwe ndi Mary Kaliati. Awiriwa akuti adakumana ali pasukulu ya Nkhoma pomwe onse ankaphunzira ndipo apa adali paulendo wopita kukaonerera masewero a timu ya Silver Strikers ndipo mwamwayi zidachitika kuti onse ankasapota timu yomweyo. Ine ndinkapita kukaonerera mpira ndiye patsogolo panga ndidaona munthu akulowera njira yomweyo. Pokhala munthu woti ndinkamuona pasukulu, ndidamuthamangira ndipo nditamufunsa komwe ankapita adandiyankha kuti adali paulendo wa kumpira, adatero Daniel. Iye adati apo awiriwo adayendera limodzi ndipo ali mnjira atazindikira kuti onse amakonda timu imodzi ubale udayambika pomwepo moti ankatengana nthawi zonse kukakhala mpira kukaonerera limodzi. Nditaona chidwi chake pampira komanso nditakhutira kuti zokonda zake ndi zanga ndi zofanana ndidaona chanzeru kuti tidzasungane ndipo nditamuuza, adagwirizana ndi maganizo anga,adatero Daniel. Mary adati iye ataona zomwe Daniel amakonda sadachotsere kuti adakumana ndi munthu yemwe angadzasungane naye popanda mavuto ndipo mwamaganizo akewo zidayendadi choncho mpaka pano akukhala limodzi ngati banja mokondwa. Zidangokhala ngati kuti ndife mapasa chifukwa zambiri zomwe ndimakonda, nayenso amakonda zomwezo monga kuleza ntima, khama pa zinthu ndi kukonda masewero ampira komanso timu yathu kukhala imodzi ndi chinthu chondisangalatsa kwambiri, adatero Mary. Awiriwa adamaliza zilinganizo zonse zoti anthu nkutengana ngati bambo ndi mayi ndipo pano ndi banja la ana atatu ndipo akuti anawonso akuyenda mmapazi mwa makolo kukonda timu ya Silver Strikers. Chikondi chomwe awiriwa ali nacho pa timu yomwe amasapotayi nchodabwitsa chifukwa akuti timuyi ikapanda kuchita bwino ngakhale chakudya onse awiri sachifuna mpaka kumatheka kugona nayo chakudya akuchiona. ",16 "Papa Wapereka Zipangizo Za Mchipatala Mdziko La Ecuador Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wapereka thandizo la zipangizo za mchipatala ku dziko la Ecuador. Malinga ndi malipoti a Vatican Radio, Papa wapereka thandizoli ngati njira imodzi yofuna kuchepetsa mavuto omwe dziko la Ecuador likukumana nao maka chifukwa cha mliri wa Coronavirus. Thandizoli ndi la zipangizo zothandiza anthu omwe akuvutika kupuma bwino kuti athe kupuma mosavutika. Bungwe la ma episkopi a Mpingo wa Katolika mdziko la Ecuador atsimikiza za nkhaniyi kazembe wa dziko la Ecuador kulikulu la Mpingo ku Vatican Jos Luis lvarez Palacio atalengeza kuti thandizoli latumizidwa kale ndipo kuti lifika mdzikolo masiku ochepa akubwerawa. Anthu 47,000 agwidwa ndi nthenda ya Covid 19 ndipo anthu 4,000 amwalira ndi nthendayi mdziko la Ecuador lomwe liri ndi chiwerengero cha anthu chokwana 17 million malinga ndi malipoti a unduna wa za umoyo mdzikolo. Thandizo la Papa Francisco ku dziko la Ecuador ndi limodzi mwa zithandize zomwe iye wakhala akupereka ku maiko osiyana-siyana omwe akhudzidwa ndi mliri wa Coronavirus. Mmbuyomu iye wapereka thandizo la zipangizo za mchipatala ku maiko a Italy, Romania, Spain, Syria, Israel, Zambia pongotchula ochepa. ",6 "T/A Kaphuka Alonjeza Kuthana ndi Miyambo Yokolezera Edzi Chipatala cha mpingo wa katolika cha Kasina mu dayosizi ya Dedza chinachita nawo mwambo wokumbukira matenda a Edzi pa dziko lonse wa chaka chino. Mwambo-wu wachitika lolemba pa bwalo la zamasewero la Nampala lomwe lili mdera la mfumu yaikulu Kaphuka. Mmau ake mkulu woyanganira zoyeza magazi pa chipatala cha Mission cha Kasina Mai Dorothy Chikafa ati nkoyenera kuti munthu aliyense adzidziwa momwe mthupi mwake mulili poyezetsa magazi. Tikupempha kwambiri abambo ambiri kuti azibwera kudzayezetsa magazi kaamba koti ngakhale anthu ali banja amatha kuthala ndi zotsatira zosiyana anatero mayi chikafa. Polankhulanso mfumu yaikulu Kaphuka ya mbomalo yomwe inali nawo ku mwambowu yati iyesetsa kulimbana ndi miyambo ina yomwe ikupitilira kukolezera kufala kwa kachilombo koyambitsa matenda a edzi ka HIV ndipo kuti aliyense yemwe apezeka akulimbikitsa miyambo yoyipayi mmudzi mwawo azilandila chilango chokhwima kuti wena atengerepo phunziro. ",6 " Kufumuka si kulakwa, olemekezeka! Nkhani ili mkamwamkamwa panopa ndi yoti nduna ya zaulimi, mthirira ndi chitukuko cha madzi, George Chaponda, kudzanso mkulu wa bungwe la Admarc, Foster Mulumbe, atule pansi maudindo awo kuti komiti yomwe Pulezidenti Peter Mutharika wakhazikitsa kuti ifufuze za nkhani ya chimanga chomwe boma lidagula kudziko la Zambia igwire bwino ntchito yake. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Chaponda wanenetsa kuti satula pansi udindo wake monga nduna. Nayenso Mulumbe wati sanenapo kanthu pankhaniyi. Chaponda wati sakuonapo chomwe adalakwa ngakhale kuti akukhudzidwa ndi nkhani yogula chimanga kuchokera kudziko la Zambia kuti chipulumutse anthu kunjala yomwe yagwa mdziko muno. Zomwe zikumveka nzakuti pakukhala ngati padalowa chinyengo malinga ndi mmene malonda a chimangawo adayendera. Izi zili choncho chifukwa mmalo mongogula chimangacho motchipa ku Zambia Cooperative Federation (ZCF) ogulitsa chimanga ku Zambia, boma la Malawi, kudzera ku bungwe la Admarc, lidaganiza zogula chimangacho pamtengo wodula pogwiritsa ntchito kampani yomwe si ya boma la Zambia yotchedwa Kaloswe Commuter and Courier Limited ngati mkhalapakati. Chifukwa chogwiritsa ntchito kampaniyo pogula chimanga chokwana matani 100 000, boma la Malawi lidasakaza ndalama zokwana K26 biliyoni zomwe lidakongola kubanki ya Eastern and Southern African and Development, lomwe limadziwikanso ngati PTA Bank. Achikhala kuti adangogula chimangacho ku ZCF, boma likadagwiritsa ndalama zokwana pafupifupi K15 biliyoni basi. Izi zikutanthauza kuti boma la Malawi lidasakaza ndalama zokwana pafupifupi K9.5 biliyoni zapamwamba pogula chimangacho kudzera kukampani ya Kaloswe Commuter and Courier Limited. Ho, zichulukirenji ndalama! Funso nkumati: Padali chifukwa chanji chosankhira njira yogula chimanga pamtengo wokwera chomwechi pomwe njira idalipo yopezera chimangacho pamtengo wotsika? Apa mpamene pakhota nyani mchira, nchifukwa chake Amalawi ambiri, kuphatikizapo a mabungwe osiyanasiyana akuganiza kuti pena pake payenera kuti padalowa chinyengowina ayenera kuti adanyambitapo kena kake! Ndikukumbukira nthawi ina yake Joe Manduwa, yemwe adali wachiwiri kwa nduna ya zaulimi nthawi ya Bakili Muluzi, ankayankha mlandundaiwala pangono kuti udali mlandu wanji poti ndi kale limene lija. Manduwa, mwa iye yekha, adatula pansi mpando wake wonona ponena kuti ankafuna kuti chilungamo chioneke bwinobwino pamlandu wake posatengera kuti wavala ministerial jacket (jekete ya uminisitala). Mwina a Chaponda ndi a Mulumbe, akadatengerapo phunziro pa zomwe adachita Manduwa potula pansi udindo kuti zofufuza ziyende myaa popanda zokayikitsa kapena zopingapinga. Ngati ofufuzawo sawapeza kulakwa pa zomwe zidachitikazo, sindikukayika kuti Pulezidenti Mutharika adzawabwezera pantchito zawo zofufuzazo zikadzatha. ",10 "Papa Wakhazikitsa Chaka cha Faustina pa Kalendala ya Mpingo Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wakhazikitsa chaka Faustina Woyera pa kalendala ya mpingo. Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican izi zadziwika kudzera mu kalata yomwe bungwe lowona za chipembedzo ndi ma sakramenti ku likulu la mpingo ku Vatican latulutsa tsiku lolemba pa 18 May. Chithunzithunzi cha Faustina Woyera Kalatayo yati Papa Francisco wakhazikitsa tsiku la 5 October pa kalendala ya mpingo wa katolika kuti likhale chaka cha Faustina Woyera. Bungwe loona za Chipembedzo ndi ma Sakramenti kulikulu la Mpingo ku Vatican (Congregation for Divine Worship and the Discipline of the Sacraments) lomwe limatsogoleredwa ndi Cardinal Robert Sarah lolemba pa 18 May lalengeza kuti Papa Francisco wakhazikitsa chaka cha Maria Faustina Kowalska pa kalendala ya Mpingo (Liturgical calendar). Malinga ndi kalata ya bungweli Papa Francisco wakhazikitsa tsiku la 5 October chaka chilichonse kukhala chaka cha Faustina Woyera. Chochititsa chidwi pa nkhaniyi nchakuti nkhaniyi yadziwika pa 18 May tsiku lomwe Mpingo umakumbukira kuti papita zaka 100 pamene Papa Yohane Paulo Wachiwiri Woyera anabadwa ku Poland ndipo ndi Papa Yohane Paulo Wachiwiriyu yemwe adakhazikitsa Faustina kukhala Woyera mchaka cha 2000. Faustina adabadwa mchaka cha 1905 ku Poland ndipo anamwalira mchaka cha 1938.Iye adali kukhala ndi asisitere a chipani cha Amayi Maria a Chifundo (Sisters of Our Lady of Mercy) Faustina adali kusinkhasinkha za chifundo cha Mulungu chotumphuka kudzera mwa Ambuye Yesu. Mapemphero osiyana-siyana a Chifundo cha Mulungu komanso laMulungu la Chifundo cha Mulungu (Divine Mercy Sunday) ndi zipatso za moyo wa Faustina Woyera yemwe anali Virgo. ",13 "Anthu ku Liwawadzi Aponya Voti Anthu a ku ward ya Liwawadzi mdera la kumpoto kwa boma la Balaka aponya voti yofuna kusankha khansala wa deralo. Chisankho cha chibwerezachi chikudza kutsatira imfa ya yemwe anasankhidwa kukhala khansala wa derali pa chisankho chomwe chinachitika mdziko muno pa 21 May 2019. Malinga ndi mtolankhani wathu amene ali ku derali, anthu ochepa ndi omwe akupita kukaponya voti yawo pa chisankhochi zomwe zikupereka chikayiko chakuti anthu ochepa ndi omwe atenge nawo gawo poponya voti pa chisankhochi. Anthu amene akupikisana pa chisankhochi alipo asanu ndi mmodzi (6) omwe ndi a Precious chimtengo omwe ndi oyima powokha, a Falao Kambiri omwe akuyimira chipani cha Democratic Progressive (DPP), a Mervin Makwinja akuyimira chipani cha Freedom, a Harris Mhere omwe akuyimira chipani cha Mbakuwaku Movement for Development (MMD), a Ronald Mphepo omwe akuyimira chipani cha Peoples (PP) komanso a Obert Peter omwe akuyima pawokha. Malinga ndi dongosolo la bungwe loyendetsa chisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC), kuponya voti kwayamba 6 koloko mmawa ndipo kukuyembekezekanso kutsekedwa nthawi ikakwana 6 koloko madzulo ndipo pambuyo pake payambe ntchito yowerengera mavotiwo. Anthu okwana 2482 ndi omwe analembetsa mu kaundula wa voti pa chisankhochi. ",11 " Veteran hymnist Nyathole buried Victoria Nqabile Thole, celebrated locally for her hymn writing skills, was buried last week in Mzimba. Coincidentally, Nyathole, as she was fondly called, was the mother of the late singer and composer Griffin Mhango, who founded Kalimba Band. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Her touch on murals Nyatholes coffin Nyathole was the daughter of Reverand PZ Thole, whose compositions appear in the Tumbuka Hymn Book. She composed numerous spiritual songs, some of which have made it into the newer edition of Tumbuka Hymns. According to her grandson, current Kalimba Band leader Vita Chirwa, Nyathole was born in 1924. She initially worked for Malawi Young Pioneers (MYP) in Mzuzu, then was transferred to Nansawa Training Base where she worked as matron under former president Bakili Muluzi who was then principal of the base. She eventually went to Ghana and later, Germany for technical training and when she returned, she helped to shape various Malawi women into productive citizens, he said. According to Chirwa, Nyathole was later transferred to MYP Headquarters in Kanjedza where she continued with her noble work until her retirement in 1975. She later became one of president Kamuzu Bandas nominated MPs for Mzimba and served two successive terms after which she quit politics and devoted her time to serving the Lord through singing and preaching, he said. She came from Elangeni Village in Mzimba where she was laid to rest. ",15 " Mgwedegwede mzipani wakula Mgwedegwede womwe wayanga chipani cholamula cha DPP ndi zina zotsutsa boma monga UDF ndi MCP ungabale zisankho zabwino mu 2014, waunikira katswiri pandale yemwenso ndi mphunzitsi wa zandale kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mkuluyu, Blessings Chinsinga, wati umu ndi mmene zimayenera kukhalira maka zisankho pulezidenti komanso a phungu zikayandikira. Apa Chinsinga wati ichi ndichiyambi chabe ndipo pena zidzifika pa alindi mwana agwiritse, koma anthu adekhe mpaka madzi atadikha kuopa kumwa matope. Iye wati misamuko ikuchitika mzipani ndi imene itamangenso zipani mwatsopano, kuzisanduliza zolimba. Sabata yatha, aphungu anayi a chipani cholamula cha DPP adauza nyuzipepala ya Weekend Nation kuti akhazikitsa gulu lomwe lidziunikira pomwe pakhota nyani mchira mchipanichi. Gululi lomwe woliyankhulira ndi phungu wa dera la kumwera kwa kwa mzinda kwa Blantyre, Moses Kunkuyu, lati pali aphungu 30 ndipo lidziuza mtsogoleri wa dziko lino Bingu wa Mutharika chindunji, osati phula lomwe ena omuzungulira akhala akukumata. Ku UDF matatalazi sakutha pomwe chipanichi chagawika pawiri. Akatakwe monga Humphrey Mvula ndi Sam Mpasu mwa ena ali pambuyo pa Friday Jumbe yemwe akugwiriziza udindo wa pulezidenti wa chipanichi kuchokera pomwe mtsogoleri wakale Bakili Muluzi adalengeza kuti wasiya ndale. Ndipo gulu lina kuli zikanthawe monga mlembi wachipanichi, Kennedy Makwangwala, Geroge Nga Ntafu, Ibrahim Matola kudzanso aphungu 15 a chipanichi ku Nyumba ya Malamulo ali pambuyo pa mwana wa Atcheya Atupele Muluzi. Pomwe ena akadziotche monga yemwe adali wachiwiri kwa mneneri wachipanichi, Ken Msonda, wasamuka mu UDF ndipo walowa chipani cha wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda cha Peoples Party [PP]. Henry Phoya, yemwe adachotsedwa mchipani cha DPP mmbuyomu nayenso waumanga ndipo walowa MCP. Phoya adakhalapo nduna mmaboma a UDF ndi DPP. Chinsinga wati zonsezi ndizosadabwitsa chifukwa zisankho zikayandikira andale amasinkhasinkha kolowera kuti adzachite bwino. Apa aliyense amayangana mazira omwe angamubalire kanthu akawafungatira. Pofika mu Juni zikhala zambiri zikuchitika pandale. Izi zikuyenera kuchitika pano chifukwa zitati zizichitika mu 2013 woponya voti angasokonekere koopsa. Pounikira pa andale angapo omwe akwawira kuzipani zina, iye wati kuyenda kwa anthuwa kungakhale ndi tanthauzo, mwinanso ayi. A Msonda adatsanzika kuti akukalera zidzukulu, koma pano akuti alowa kuchipani cha PP. Izi sizingapatse anthu chikhulupiriro mwa mkuluyu. Zomwe achita a Phoya zadabwitsa ambiri, ngakhale inenso. Koma izi mwina zingasinthe zingapo pandale malinga ndi momwe anthu amachionera chipani ca MCP. Nkutheka a Phoya abweretsa zingapo ku MCP chifukwa cha kulimba mtima kwawo komwe adaonetsa potsutsa mabilo oipa mnyumba ya malamulo, akutero Chinsinga. Baziliyo Kajani wa mmudzi mwa Chaponya kwa T/A Mzukuzuku mboma la Mzimba wati, sakuganiza kuti mpungwepungwewu ungakonze masankho a mu 2014 kaamba koti nthawi ino ndiyoyenera kuti zipani zotsutsa zizichita ntchito yachitukuko. Pandale pamafunika kukhala mgwirizano ncholinga chotukula dziko, osati zikuchitikazi zomwe sizingatipindulire. Zipani zotsutsa zikuyenera kupereka thandizo kuchipani cholamula, maka pankhani ya chitukuko, zomwe sizikuchitika. Izi zingadzabale ziwawa mu 2014, adatero Kajani. Frank Mpuno wa mmudzi mwa Yoyola kwa T/A Masasa mboma la Ntcheu wati masankho abwino mu 2014 angadze ngati akuluakulu a zipani akudziwitsa anthu za zomwe zikuchitikazo. Amatifuna panthawi ya kampeni basi. Mukadzamva kuti sitikavota osamadabwa, akutero Mpuyo. Mgwedegwede mu UDF udayamba mmwezi wa Okutobala 2011 pomwe Atupele Muluzi adabwera poyera ndikulengeza kuti iye adzaima nawo pa mpando wa pulezidenti mchaka cha 2014. Izi sizidakomere komiti yaikulu mchipanichi ndipo akuluakulu mmenemo adati izi nzosemphana ndi malamulo achipani. Apa chipanichi chidaitanitsa Atupele kuti akaonekere ku komiti yosungitsa mwambo yachipanichi koma iye adakana ndipo chidamuchotsa. Kugwedezekaku kudabukanso pa 21 Disembala 2011 pomwe mlembi wachipanichi Kennedy Makwangwala adalemba kalata yothetsa maudindo onse. Kulumana ku MCP kuli pakati pa mlembi wa chipanichi, Chris Daza, ndi mtsogoleri wachipani, John Tembo. Daza wakhala akulankhula poyera kuti Tembo akuyenera kusiira utsogoleri wachipanichi mmanja mwa achinyamata, zomwe zakhala zikutsutsula Tembo. Mmwezi wa Sepitembala chaka chatha, komiti yaikulu ya chipanichi idachotsa Daza kuti sindiyenso mlembi wachipanichi koma bwalo lamilandu lalikulu ku Lilongwe mmwezi wa Okutobala lidabwezeretsa Daza pa mpandowo. Pano chipanichi chalandira Phoya. Ku DPP kwachoka aphungu angapo monga Jennifer Chilunga wa ku Zomba Nsondole yemwe adalowa chipani cha PP komanso Grace Maseko wa ku Zomba Changalume. ",11 " Anatchereza Kodi nditani? Gogo Natchereza Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndine mtsikana wa zaka 25 ndipo ndakhala pa chibwenzi ndi mnyamata wina kwa zaka zinayi. Mnyamatayu ali ndi nyumba yake ndipo akugwira ntchito yabwino pa kampani ina yopanga mafuta wophikira mu mzinda wa Lilongwe. Tidagwirizana kuti tidzakwatirana, koma mnzanga ndikamufunsa za banja amangozengereza. Kumuuza kuti apite kwathu akaonekere amangoti ndidzapitabe mpaka zaka nkumatha. Gogo, kodi pamenepa nditani popeza mnyamatayu ndimamukonda ndi mtima wanga wonse? JPJ Lilongwe JPJ Nkhaniyi siyachilendo. Atsikana ambiri amadandaula kuti anyamata adawauza kuti adzawakwatira, koma akuchulutsa njomba. Mnyamata wofuna banja sasowa. Sazengereza mwayi wokaonekera kwa makolo a mtsikana ukapezeka. Anyamata ambiri safuna banja. Amangofuna kugona ndi atsikana moti chakumtima kwawo chikapwa amawasiya nkupeza ena kumene kuli kulakwa. Muunikeni bwino bwenzi lanu kuopa kudzanongoneza bondo mtsogolo. Paja amati mtsinje wa tinkanena udakathera msiizi. Gogo Natchereza Makolo ake akukana Ndine mtsikana wa zaka 23 ndipo ndili ndi mwana mmodzi. Mnyamata wina adandiuza kuti akundifuna chibwenzi ndi cholinga choti adzandikwatire mtsogolo ndipo ndidalola. Koma makolo ndi abale ake amamukaniza kuti asakwatiwe ndi mtsikana wa mwana moti panopa zochita za bwenzi langa sindikuziona bwino. Ndikamuimbira foni nthawi zina sayankha. Ndikamutumizira uthenga pa WhatsApp umaonetsa kuti waona, koma sayankha. Gogo, mutu wanga wazungulira nditani? APA APA Usadandaule, ungozivomereza. Makolo ena amaletsa ana awo kukwatiwa ndi atsikana oti adaberekapo kumene kuli kulakwa. Anthu awiri akakondana zenizeni saona zoti wina ali ndi mwana kapena ayi. Apa zikuonetsa kuti mnyamatayo wamvera zonena za makolo ake. Choncho kutha kukhala kovuta kuti chibwenzi chanu chipitirire. Limba mtima, mudzapeza mnyamata wokukondani posatengere kuti mudaberekapo. Usada nkhawa. Chachikulu ndi kudekha. Sunga khosi mkanda woyera udzavale. ",12 "Tauni ya Mangochi Idakali ndi Misewu ya Fumbi Wolemba: Thokozani Chapola Phungu wa kunyumba ya malamulo wadera la pakati mboma la Mangochi, Victoria Kingstone wadandaula kaamba ka kuipa kwa misewu yozungulira tawuni ya Mangochi. Kingstone: Ndapempha kale ku boma ndipo a nduna alonjeza kuti akonza misewuyi Padakali pano misewuyi ndi ya fumbi ndipo nthawi ya mvula imakhala ndi matope kaamba koti ilibe phula zomwe malinga ndi iye sizoyenera mu tawuni yomwe posachedwapa ikhale mzinda. Pamenepa iye wati wakambirana ndi a unduna woona za maboma aangono ndi chitukuko chakumidzi kuti misewuyi ikonzedwe poyika phula. Nditapita ku nyumba ya malamulo ndinapempha ndipo olemekezeka a Ben Phiri omwe ndi a nduna a za maboma aangono andiyankha kale kuti mzaka zikubwerazi misewu yonse ya pa boma ikhala ndi tala, anatero Kingstone Kingstone amalankhula izi pa msonkhano womwe anachititsa pa sukulu ya pulaimale ya Milambe womwe cholinga chake chinali kuthokoza anthu omwe anamusankha pa udindowu. Iye wati zimenezi zithandizanso popititsa patsogolo ntchito zokopa alendo mbomalo polingaliranso kuti boma lili ndi malingaliro omanga hotela yapamwamba komanso bwalo la ndege mbomalo. Izi zikudza patapita pafupifupi chaka pomwe anthu ochita bizinesi ya kabaza mbomalo anachita ziwonetsero pofuna kukakamiza akuluakulu a khonsoloyo kuti akonze misewu yozungulira tauniyi zomwe sizinachitikebe mpakana padakalipano. Pa za tsikuli iye wati anawona kuti ndi koyenera kuti apite ku dera kwake ndi kukathokoza anthu omwe anamusankha pa udindowu ndi kudya komanso kusangalala nawo limodzi. Iye anati achita miyambo ya ngati imeneyi mmalo onse oponyera voti a mu dera lake omwe alipo okwana 25. Patsikuli mwazina iye anakumbutsanso anthuwa za malonjezo ake omwe anali akuchita mu nyengo yokopa anthu kuti azamuvotere zomwe anawatsimikizira kuti zichitikadi. Chimodzi mwa icho ndinawalonjeza amayi kuti theka la malipiro anga lizipita kwa iwowo. Pano ndikuwatsimikizira kuti ndalama zomwe zikubwera mwezi uno theka lake ndiwapatsa kuti azichitira bizinesi, anatero Kingstone. ",11 " DPP madzi afika mkhosiMuntali Zipani zotsutsa zati nzodabwa kuti boma lagundika kukweza anthu ogwira ntchito mboma, komanso kulipira mafumu nthawi ino ya kampeni pamene mmbuyo monsemu akhala akudandaula koma samathandizidwa. Mwezi umodzi wokha boma lakweza apunzitsi 20 000, apolisi 7 000 moti padakali pano lili mkati molipira mafumu 42 000 ndalama za miyezi 6 zomwe zidatsalira chaka chatha. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Otsutsa akuti chipani cha DPP chikunyengerera mafumu kuti adzachivotere Boma ligwiritsa ntchito K832 miliyoni polipira mafumuwo. Zipani zotsutsa zati zikuona kuti chipani cholamula cha Democratic Progressive (DPP) chikungofuna kugwiritsa ntchito ndondomeko zaboma pochita kampeni. Koma mneneri wa boma Henry Musa adati sakuonapo vuto lililonse chifukwa palibe lamulo lomwe limafotokoza nthawi yokwezera anthu pantchito kapena kulipira mafumu. Anthu ogwira ntchito mboma akhala akukwezedwa, komanso mafumu akhala akulipidwa mmaulamuliro onse omwe akhalapo. Choseketsa nchoti palibe lamulo lomwe lifotokoza nthawi yokwezera ogwira ntchito kapena kulipilira mafumu, adatero Mussa. Mfumu Chindi ya ku Mzimba, Chadza ya ku Lilongwe ndi Dambe ya ku Neno yatsimikizira Tamvani kuti mafumu alandira mswahara wa June mpaka December 2018. Mneneri wa unduna wa maboma angonoangono ndi chitukuko cha mmidzi Muhlabase Mughogho adati ndalamazi nzomwe boma limayenera kuonjezera pa mswahara wa mafumuwo kuchokera pomwe Nyumba ya Malamulo idakweza mswaharawo. Nyumba ya Malamulo idavomereza kuti mswahara wa mafumu ukwere ndi K100 pa K1 000 iliyonse koma kuyambira mwezi wa June mpaka December 2018, mafumu samalandira ndalama yoonjezerayo ndiye akupatsidwa pano, adatero Mughogho. Mlembi wamkulu wa chipani cha UTM Patricia Kaliati adati ndiwodabwa kuti kuonjezera mswahara wa mafumu kutavomerezedwa, aphungu adaika mbajeti ndiye nchifukwa chiyani samapatsidwa ndalama zonse? Apatu ndikuona kuti boma limazunza dala mafumu kuti pambuyo pake adzawatseke mmaso nthawi ya kampeni. Uku nkulakwa chifukwa panthawiyo akadatha kupanga ndondomeko zina, adatero Kaliati. Koma iye adati ndiwokondwa kuti mafumuwo alandira ndalama zawo zomwe adagwirira ntchito ngakhale azilandira nthawi yolakwika. Kaliati adati ndalamazo nzofunika kuonjezeranso chifukwa nzochepa poyerekeza ndi ntchito yomwe mafumu amagwira. Mawuwa akugwirizana ndi omwe adalankhula mtsogoleri wa chipani cha Malawi Congress (MCP) Lazarus Chakwera pa msonkhano wake wa ku Kasiya kuti mswahara wa mafumu ndiwofunika kuganiziridwa, komanso azipatsidwa mu nthawi yake. Mneneri wa MCP Maurice Munthali adati zomwe zikuchitikazi zikusonyeza kuti chipani cha DPP chapanikizika chifukwa cholephera kuchita zinthu mu nthawi yake. Kodi aphunzitsi amayenera kukwezedwa liti? Nanga mafumu amayenera kulandira liti ndalamazo? Panopa madzi ali mkhosi ndiye akufuna awanamize? Ayi sititero, adatero Munthali. Iye adati aphunzitsi ndi apolisi omwe akwezedwawo awonetsetse kuti zofunikira zonse zatheka kuti wina asadzawakanire mawa, komanso mafumu alandire ndalama zawo koma zisawasokoneze pokavota, adatero Munthali. Mlembi wamkulu wa chipani cha United Democratic Front (UDF) Kandi Padambo adati boma lifotokozere bwino mafumu ndi anthu komwe kwachokera ndalamazo chifukwa ena akhoza kumaona ngati DPP ndiyo yapereka. Katswiri pa ndale George Phiri adati Mussa akunena zoona kuti palibe lamulo lofotokoza nthawi yokwezera munthu kapena kumulipira malipiro ake, koma pali ndondomeko zina zomwe zimayenera kutsatidwa zomwe akuona kuti sizidatsatidwe. Choyamba munthu amakwenzedwa akagwira bwino ntchito. Nzowona kuti aphunzitsi ndi apolisi onsewa akugwira bwino ntchito yawo? Chachiwiri adziwa liti kuti akuyenera kukwenzedwa pa ntchito? adatero Phiri. Iye adati nkhaniyi ikapanda kuunikidwa bwino, idzabweretsa mavuto aakulu patsogolo makamaka ngati sipakhala makalata a umboni oti anthu akukwezedwadi pa ntchito. ",11 "Atumiki a Dayosizi ya Dedza Asulidwa za Chibalalitso Wolemba: Thokozani Chapola Mkulu owona za utumiki mu dayosizi ya DEDZA bambo Peter White, lachisanu lapitali ati ati msulo wowakonzekeretsa ansembe ndi a sisiteri za chaka cha chibalalitso cha mpingo umathandiza kuzindikiritsa atumikiwa ntchito yomwe ali nayo mu mpingowu. Bambo WHITE omwe ndi mkulu oyanganira za utumiki mu dayosiziyi amalankhula izi pa maphunziro a tsiku limodzi omwe anakonzedwa ndi office yoona za mabungwe a utumiki wa apapa mu dayosiziyi. Tinawona kuti ndi kofunika kuwasula atumikiwa chifukwa iwo ndi amene amakhala patsogolo kutsogelera ma parishi awo choncho akamvetsa bwino za chibalalitso cha mpingo zikathandizanso pomema akhristu kuti apereke molowa manja pa tsikuli, anatero bambo White. Mmawu ake mkulu wa mabungwe a utumiki wa apapa mu dayosizi ya DEDZA, bambo PETER MADEYA ati office yawo inakonza maphunzirowa kuti ansembe athe kuzindikira bwino za chibalalitso cha mpingo komanso athe kuzindikiritsa akhristu zimene a Papa akufuna mu uthenga wawo wa chaka chino. Zithandizanso atumikiwa kumvetsa zambiri za mabungwe a utumiki wa a Papa, anatero bambo Madeya. Mwambo waukulu wa chaka cha chibalalitso mu mpingo wa katolika mdziko muno uchitikira ku St. Pius Parish mu arkidayosizi ya Blantyre pa 13 October 2019. ",13 "Anjatidwa Kamba Kogona ndi Galu Apolisi mboma la Mchinji amanga mamuna wina wa zaka 20 zakubadwa Glandisoni Feliyala kaamba komuganidzira kuti anachita zadama ndi galu. Wofalitsa nkhani za apolisi mbomalo, Inspector Kaitano Lubrino wati mkuluyu anapezeleredwa ndi mkazi wake akuchita zadama ndi galu usiku wapa 27 December 2019. Mkazi wake atamuuza kuti akagone anakana ndipo mayiyo anakalowa yekha mnyumba koma atawona kuchedwa anaganiza zotuluka kuti awone chomwe chachitika kwa mamuna wakeyo ndipo ndi pomwe anamupeza akugona ndi galu. Anayitana Anthu ena oyandikana nawo ndipo anthuwa anamugwira mkuluyu ndi kumupititsa ku polisi, anatero Inspecto Lubrino. Inspector Lubrino wati a Feliyala anauza apolisi kuti iwo adawudzidwa ndi nsinganga wina wa ku Karonga kuti ngati akufuna kulemera agone ndi galu ngati chizimba. A Glandisoni Feliyala ali ndi zaka 20 ndipo amachokera mmudzi mwa Malewa, T/A Gumba mboma la Mchinji ndipo akuyembekedzereka kukawonekera ku bwalo la milandu posachedwapa. ",14 "Papa Wati Akhristu Apemphelere Atsogoleri Wolemba: Glory Kondowe 9/08/francis.jpg 308w"" sizes=""(max-width: 512px) 100vw, 512px"" />Wapempha anthu apemphelere atsogoleri-Papa Francisko Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisko lero wati ndi kofunika kumapempherera atsogoleri a boma komanso a ndale. Iye walankhura izi pamwambo wa misa yomwe anatsogolera ku likulu la mpingowu ku Vatican. Malinga ndi Papa Francisko koyenera kumawapemphelera atsogoleriwa nthawi zonse ndi cholinga choti atumikire anthu awo moyenera poyanganira za udindo omwe amasenza. Mwazina mtsogoleriyu anagwira mau a mkalata yoyamba ya Paulo Woyera kwa Timoteyo 2 ndime ya 1 mpaka 8 onena za kufunika kopemphelera mafumu ndi onse olamulira. Iye wati nthawi zina atsogoleri amayamikiridwa komanso kunyozedwa ndipo Papa wati zimenezi sizinasiye malo popeza ngakhale atsogoleri a mpingo monga ansembe, a episikopi komaso asiteri amayamikilidwa komanso kunyozedwa choncho ndi kofunika kuwapemphelera nthawi ndi nthawi kuti apitilize ntchito zawo ndikukhala atsogoleri abwino nthawi zonse. ",13 "Milandu Yogwililira Yakwera Mboma la Zomba Mkulu wa apolisi chigawo chaku mmawa kwa dziko lino Commissioner Arlene Baluwa wapempha anthu mdziko muno kuti athandizane ndi polisi pa ntchito yothana ndi mchitidwe wogwilira ana mdziko muno. Wati milandu yogwililira yakwera kwambiri-Baluwa Commissioner Baluwa amayankhula izi kwa Group Village Headman Chingondo, mdera la mfumu yayikulu Mwambo mboma la Zomba pa msonkhano womwe apolisi anakonza okambirana ndi anthu za momwe angathetsere nkhanza zogwilira ndi kuzunza anthu okalamba kuphatikizapo anthu a khungu la chi-albino. Commissioner Baluwa wati nkhanza zogwilira zikuchulukira mboma la Zomba kamba koti mchaka cha 2019 milandu yokwana 97 idalembetsedwa kusiyana ndi milandu 68 yomwe idalembetsedwa chaka cha 2018. Choncho Iwo apempha anthu kuti adzikanena ku polisi za nkhadza zogwililira zomwe zikuchitika pakati pa magulu okhudzidwawa. Pa nkhani ya belo ya polisi Commissioner Baluwa wati anthu akuyenera kudziwa kuti beloyi ndi yaulele kotero sakumayenera kupereka ndalama ina iliyonso kwa apolisi pomwe apempha belo. ",14 " Titsirika nkhalango zonseNganga Gulu lina la asinganga ku Dedza ladzithemba kuti likhoza kuteteza nkhalango za dziko lino ndi chambu koma akuluakulu a boma ati zonse zili mmanja mwa asingangawo kuti awakhutitse kuti njirayo idzayenda. Mkulu woyanganira za nkhalango mdziko muno Clement Chilima adati nthambiyo ndi yokonzeka kupereka mpata kwa asingangawo kugwira ntchito ndi asingangawo poteteza nkhalangozo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Kodi nsupa ndi zitsamba zingathandize kuteteza nkhalango? Iye adati chomwe asingangawa angachite nkulembera kalata nthambiyo kuti ifunse upangiri pena ndi pena koma ganizo lawolo ndi lolandiridwa ngati silikuphwanya malamulo. Mmagwiridwe a ntchito yathu, timalandira aliyense yemwe ali ndi njira yothandiza. Ngati asingangawa akunena zoona ndipo njira yawoyo siyikuphwanya malamulo, abwere tiwapatsa mpata, adatero Chilima. Mkulu wa nthambi yoteteza nyama za kutchire Brighton Kumchedwa adati sanganeneretu mwa ndithendithe kuti chambu ndiye yankho koma adati gulu la asingangalo ndilolandiridwa ngati likudziwadi njira yomwe ingathandize kuteteza nkhalango. Ntchito yathu ndi yogwira ndi anthu ndiye ngati papezeka ena omwe akuti ali ndi njira yomwe ingathandize, chowaletsera nchiyani? Atatipeza nkutifotokozera bwinobwino, ndipo titamvetsa, tikhoza kuona kuti tingagwire nawo bwanji ntchito, adatero Kumchedwa. Iye adati mdziko muno muli nkhalango 84 zomwe zimafunika chitetezo chifukwa mitengo ndi nyama zopezeka mmenemo zikutha mosakhala bwino chifukwa cha mbala. Gulu la asingangali ndi lochokera mboma la Dedza ndipo lanenetsa kuti chambu chikhoza kugwira ntchito yoteteza nkhalango kuposa ntchito ya alonda ndi asilikali. Nthambi ya za nkhalango ndi nyama zopezeka mmenemo, itaima mutu ndi mchitidwe opha nyama komanso kudula mitengo mozemba, idalemba alonda omwe amathandizana ndi asilikali kuteteza nkhalango ndi nyama. Woyanganira ndi kulangiza asinganga pantchito yawo mboma la Dedza, Gulupu Ntambeni Chinyamula adati kupatula chidima, ophotchola mnkhalango akhoza kukakamiraa mpaka kugwidwa momwemo. Chambu nchamphamvu zedi chikhoza kugwira munthu yemwe amafuna kukasokoneza mnkhalango mpaka kugwidwa momwemo nkulandira chilango choyenera, adatero Chinyamula. Pulezidenti wa asinganga a mdziko muno Frank Manyowa adati nzotheka kuteteza nkhalangozi potsirika nkhalangozo ndi chambu mmalo modalira alonda ndi asilikali. Ndi chambu, tikhoza kuteteza nkhalango zonse zomwe zikusowa chitetezo kuti owonongawo asamazione powakantha ndi chidima ndipo akhoza kulephera kupanga upandu omwe adakonzawo, adatero Manyowa. Iye adati asinganga ali ndi njira zambiri zomwe akhonza kulangira anthu oononga nkhalango ndipo zilangozo zikhoza kuwapatsa mantha moti sangalakelake kubwerera kunkhalango. Manyowa adati asinganga zimawapweteka nkhalango zikamaonongeka chifukwa kasupe wa ntchito yawo wagona mmenemo. Timalimbikitsa kuteteza nkhalango chifukwa ndiko timapeza mankhwala athu. Boma lakhala likuyesetsa kuteteza nkhalango koma zikuwoneka kuti zikuvuta koma asinganga akhoza kukwanitsa ndi chambu, iye adatero. ",19 " Mkazi wansanje achekacheka mnzake Bwalo la milandu la majisitireti ku Mchinji masiku apitawa lidalamula kuti mayi wansanje amene adachekacheka mayi mnzake ndi mpeni pakhosi ndi kunkhope akagwire jere la miyezi 12 koma lidamumasula ponena kuti asadzapezekenso ndi mlandu wina kwa chaka chimodzi ndi theka. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Woimira boma pamilandu, Thom Waya, adauza bwalolo kuti mkazi wansanjeyo, Chimwemwe Fanizo, wa zaka 21, adafuna kuvulaza mwana wa mkazi mnzake wa miyezi 7 ndi mpeni ati popeza mwamuna wake ankapereka thandizo kwa mwanayo. Wasiya kuonetsa mabala ake mchipatala Waya adati mpeniwo udasempha mwanayo yemwe adali kumsana ndi kulunjika pakhosi la mayi ake. Mbereko yomwe adaberekera mwanayo idamasuka moti adagwa pansi ndipo achisoni adamutola ndi kuthawa naye. Izi sizidakondweretse Fanizo, yemwe adalikumba liwiro kuthamangitsa munthu amene adathawitsa mwanayo, mpeni uli mmanja. Komatu apa nkuti mkaziyo atamuchekacheka mnzakeyo malo anayi. Anthu adamugwira ndipo adapita naye kupolisi pamodzi ndi wovulazidwayo. Izi zidachitika mmawa wa pa 6 January pa Mkanda Trading Centre. Apolisi adamutsekulira mlandu wovulaza munthu, womwe womangidwayo adauvomera pamaso pa woweruza, majisitireti Rodwell Meja. Malinga ndi Waya, bwalolo silidachedwe kugamula mlanduwo chifukwa woimbidwa mlandu sadatayitse khotilo nthawi povomera kulakwa. Podandaulira bwalolo kuti limuganizire popereka chilango, Fanizo adati adapalamula mlanduwo chifukwa adachita kuputidwa ndi wodandaulayo, Tsala Wasiya, pokhala pachibwenzi ndi mwamuna wake. Pogamula mlanduwo, Meja adati bwalo lake lidamupeza ndi mlandu wovulaza ndipo ayenera kulangidwa molingana ndi malamulo a dziko lino, koma adapereka chilango chosakhwimacho poganizira kuti adachita kuputidwa komanso poti sadatayitse bwalolo nthawi povomereza kulakwa kwake. Meja adapereka chilango choti Fanizo akaseweze chaka chimodzi kundende koma adati kundendeko sapitako bola asapezekenso ndi mlandu kwa miyezi 18. Adamulola kuti azipita kwawo, mlandu watha. Adatinso ngati sakukhutira chi chigamulocho ali ndi ufulu kuchita apilo. Msangulutso udacheza ndi Wasiya, yemwe ali ndi zaka 20, kuti umve mbali yake ndi mmene zidakhalira kuti zifike mpakana kuvulazidwa chonchi. Iye adati adalidi paubwenzi ndi Daniel Nkhomo ndipo ubwenziwu utafumbira adapezeka ndi pakati. Iye adati ngakhale awiriwa sadalowane, Nkhomo adali kupereka chisamaliro chonse chomwe munthu oyembekezera amafuna mpaka mwana adabadwa. Koma ndidadabwa kuti pomwe mwana wanga adakwanitsa sabata zitatu, abambowa adakatenga mkazi wina kwa Msundwe ndipo adasiya kupereka chithandizo, iye adatero. Wasiya adati koma patadutsa miyezi iwiri bamboyu adayambiranso kuthandiza mwana wakeyu ndipo awiriwa amatchayirana lamya mwanayu akadwala zomwe sizimamkomera mkazi mnzakeyo. Tsiku lina ndidatumiza uthenga palamya kuti andiimbire kaamba koti mwana adali atadwala matenda otsekula mmimba. Mkazi wakeyu ndiye adandiimbira ndi kunditukwana, Wasiya adatero. Iye adati mphuno salota sadadziwe kuti Fanizo adali ndi mangawa ndipo adakagula mpeni ndi kukanoletsa kumatchini ndi cholinga chofuna kuthana naye. Wasiya adati patsikuli adali akuchokera kumsika ndipo Fanizo adamutchingira kutsogolo. Adandifunsa kuti bwanji ndimaimba lamya ya mwamuna wake? Bwanji adandisiya ine nkutenga iyeyo ngati ndili naye mwana wake? Nkudzati ndipanga za iwe, pompo mpeni sololu kuti abaye mwana kumsana. Mpeniwu udafikira pakhosi panga, adalongosola Wasiya Iye adati koma adali wodabwa kuti ngakhale adavulazidwa chomwechi Fanizo ndi mfulu ndipo adampititsa kwawo. Msangulutso udachezanso ndi Wasiya Titus, bambo wa mayi wovulazidwayu. Iye adati sakudziwa kuti mlanduwu uli pati kaamba koti atafufuza kupolisi ya Mchinji adauzidwa kuti Fanizo adamasulidwa ndi abwalo la milandu. Abwalo la milandu sadamve mbali ya mwana wanga yemwe sakupezabe bwino, kodi adamtulutsa bwanji ife okhudzidwa kulibe? Komabe ndipita konko kuti ndikamve umo zidayendera, adatero Titus. Pakalipano Wasiya wanenetsa kuti zivute motani akufuna mwamunayu amukwatire basi. Ine ndikufuna mwamunayu andikwatire chifukwa wandipatsitsa mabala, moti amuna ena sadzandisiriranso ayi. Ndipo mkazi wakeyu achita bwanji nsanje ndi ine, popeza ine ndiye ndidali woyamba ndipo ndimafunika kuchita nsanjezo ndineyo osati iyeyo wachiwiri ayi, adalankhula motsindika Wasiya. Pomwe Msangulutso udacheza ndi mwamunayo Lachinayi lapitali palamya, iye adati Wasiya adali mkazi wachibwenzi pomwe Fanizo adali wapanyumba. ",7 "Radio Maria Yalimbikitsa Omvera Ake Kuti Asatope Kuithandiza Mnyengo ya Coronavirus Radio Maria Malawi yalimbikitsa omvera ake, kuti asasiye kuthandiza wayilesiyi ndi thandizo lililonse lomwe angakhale nalo, kuti ntchito zake, zipitilire kuyenda bwino pomwe matenda a COVID -19 ayimitsa ntchito zambiri mdziko muno. Phiri: Coronavirus wayimitsa zokonzekera zonse Mkulu oyendetsa ntchito za wayilesiyi Louis Phiri, ndiyemwe wanena izi pomwe amalankhulapo pa momwe matendawa asokonezera zokonzekera za nyengo ya Mariatona yomwe imayenera kuyamba la Mulungu likudzali pa 3 May. Iye wati zokonzekera za nyengoyi zidayima kaye mpaka mtsogolomu, ndipo pano akhristu komanso ena onse akufuna kwabwino omwe amakonda kumvera wayilesiyi, akuyenera kuti atenge udindo waukulu othandiza wailesiyi kuti ntchito zake zipite patsogolo. Kuno ku Radio Maria tinali ndi malingaliro oti tikatsegulire Mariatona ku Lutchenza koma chifukwa cha mliri wa Coronavirus wu takanika kutero, anatero Phiri. ",13 "Papa Walengeza Zakusintha kwa Tsiku la Chaka cha Achinyamata Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco walengeza kuti chaka cha achinyamata (World Youth Day) chidzachitike kutsogoloku osati mmene adakonzera poyamba. Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican, Papa Francisco wavomereza kuti Chaka Cha Achinyamata (World Youth Day) komanso Chaka Cha Mabanja (World Meeting of Families) zisachitike mmene adakonzera poyamba malinga ndi nthenda ya COVID-19. Uthengawo wati malinga ndi mmene zinthu ziliri padakali pano, Chaka Cha Mabanja chomwe chimayenera kudzachitika mwezi wa June 2021 ku Rome, chidzachitike mwezi wa June mchaka cha 2022 ku Rome komweko ndipo kuti Chaka Cha a Chinyamata chomwe chimayenera kudzakhalapo chaka cha 2022 ku Lisbon mdziko la Portugal chidzachitika mu August mchaka cha 2023 ku Portugal komweko. Malinga ndi uthengawo, mliri wa Coronavirus mwa zina wasokoneza zokonzekera zomwe zimayenera kukhala zitayamba kuchitika mma Diocese a Mpingo wa Katolika pa dziko lonse komanso zokonzekera zomwe zimayenera kukhala zitayamba kuchitika padakali pano kulikulu la Mpingo ku Vatican. Chaka Cha Mabanja chimasonkhanitsa pamodzi mabanja a chikatolika kuchokera mbali zonse za dziko la pansi ndi cholinga chofuna kukondwerera moyo wa banja pakati pa mamuna ndi mkazi ndipo izi zinayamba mchaka cha 1994 pamene Chaka Cha a Chinyamata chimasonkhanitsa a chinyamata a Mpingo wa Katolika kuchokera mbali zonse za dziko la pansi pofuna kulimbikitsa a chinyamatawa pa moyo wao wa chikhristu. Papa Yohane Paulo Wachiwiri Woyera ndiye adayambitsa Chaka Cha a Chinyamata mchaka cha 1985. ",14 " Ayamba kugawa makuponi Nduna ya malimidwe Joseph Mwanamvekha yapempha alimi kuti asagulitse makuponi awo amene boma lidayamba kupereka Lachinayi. Ndunayo idakhazikitsa ntchito yopereka makuponi 4 miliyoni kwa alimi 1 miliyoni ogulira mbewu ndi feteleza pasukulu ya Mtaya mboma la Balaka. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Nduna ya malimidwe Joseph Mwanamvekha adalangizanso mafumu ndi ena okhudzidwa ndi kugawa makuponi kuti apewe kuba ndi chinyengo pantchitoyi monga zakhala zikukhalira mmbuyomu. Ndikunena pano, anthu 58 amene adagwidwa pamilandu ya makuponi chaka chatha. Amene ayerekeze kuba makuponi, lamulo lidzagwira ntchito, adatero Mwanamvekha. Iye adapempha alimi kuti ayambe kukonza mminda yawo kuti azabzale ndi mvula yoyamba chifukwa feteleza afika kumadera mnthawi yake. Chaka chino, makampani amene akugulitsa mbewu ndi feteleza mmaboma onse atitsimikizira kuti afika mnthawi yake mmadera onse. Tikufuna anthu akangolandira makuponi, nthawi yomweyo agule zipangizo, adatero Mwanamvekha. Mmbuyomu, alimi akhala akudandaula chifukwa makuponi amawaolera mmanja kaamba kosowa kokagula zipangizo zotsika mtengo. Phungu wa dera la kummawa cha pakati mbomalo Yaumi Mpaweni adapempha alimi kuti agwiritse ntchito makuponi amene alandire. Si bwino kugulitsa makuponi anu chifukwa uko ndi kudzipha. Kuti mukolole zokwanira, ndi bwino kuwagwiritsa bwino ntchito, adatero Mpaweni. Mwa zina, chaka chino kuponi iliyonse izikhala ndi nkhope ya woyenera kulandira ndi cholinga choti munthu wina asagwiritse ntchito. Makuponi 4 miliyoni ogulira zipangizo zotsika mtengo adafika mdziko muno mwezi watha ndipo aperekedwa kwa alimi 1 miliyoni mchilinganizochi chaka chino. Mndondomeko ya zachuma ya chaka chino mpaka chaka chamawa, boma lidapereka K151 biliyoni ku unduna wa malimidwe ndipo K42 biliyoni ipita ku ntchito ya makuponi. ",4 " Apolisi mbweee! ku PAC Kwa munthu wongofika kumene mumzinda wa Blantyre, ngakhale nzika za mzindawu, sabata imene yangothayi kudali chitetezo chokhwima zedi pomwe apolisi adali ponseponse. Kuyambira mmawa, apolisi adali ndi ma rodibuloku adzidzidzi mmadera ena. Mmodzi mwa anthu okhala ku Machinjiri, Leston Kampira, Lachitatu adati adadabwa ndi mndandanda wa galimoto umene udalipo pa Wenela. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Tidayenda pangonopang;ono mpaka kukafika pa Wenela kuchoka pa HHI. Tidapeza kuti apolisi amaimitsa galimoto iliyonse ndikuchita chipikisheni kubuti. Ati apolisi amaopa kuti anthu ena apita ndi zida kumsonkhano wa PAC [Public Affairs Committee], adatero iye. Msonkhano wa bungwe lounikira momwe dziko lino likuyendera la PAC udali kuchitika ku Sunbird Mount Soche ndipo usanayambe mlangizi wa pulezidenti pa zochitika mdziko muno Hetherwick Ntaba adati boma limadziwa kuti pali anthu 300 amene amakonza zipolowe msonkhano wa PAC ukangotha. Msonkhanowo udaliko Lachitatu ndi Lachinayi. Ndipo Kumbukani Mhlanga wa ku Chinyonga adati adadabwa kuona apolisi akuimika galimoto iliyonse yolowa mtauni. Zidatichedwetsa ku ntchito. Ndipo ndimadabwa kuti chikuchitika nchiyani ndisanamve kuti kuli msonkhano wa PAC, adatero iye. Kuchuluka kwa apolisi sikudali mmisewu mokha, ngakhalenso kuhotelayo, apolisi adali mbweee, ena atanyamula mfuti zawo. Pa gulu la apolisi omwe anali ku msonkhanowo, oitanidwa ndi PAC adali 6 okha, malinga ndi mkulu wabungwelo Robert Phiri. Koma Phiri adati kuonjezereka kwa apolisiwo sikunasokoneze dongosolo lawo chifukwa adakonzekera. Tidadziwa kuti apolisi abwera ochuluka potengera nkhani zomwe zidamveka za chisokonezo. Mwina nthumwi zina zidasokonezeka, koma ife tachita mmene tidakonzera, adatero Phiri. Mmodzi mwa nthumwi ku msonkhanowo, mkulu wa bungwe la Peoples Land Organisation (PLO) Vincent Wandale adati anthu adadabwa ndi gululi, koma adamasuka kukamba zotukula dziko. Zidali ngati dziko likulamulidwa ndi apolisi. Nthumwi zaboma zidabwera zambiri, sitikudziwa kuti amaopa chiyani. Ubwino wake aliyense adapereka mfundo zimene adakonza. Zoopa apolisi zidali kale ndipo sitidanjenjemere kupezeka kwawo, adatero Wandale. Mneneri wa polisi mdziko muno James Kadadzera adati kuchuluka kwa apolisi sikudali kuopseza anthu koma kupereka chitetezo. Ndife osangalala kuti msonkhano watha popanda zovuta zili zonse. Timapezeka pofunika chitetezo kuti aliyense agwire ntchito yake mosaphwanya lamulo osati kuopseza. Ndipo okonda dziko lake sanganene kuti apolisi adalakwitsa, adatero Kadadzera. Chitetezo chapolisi chokhwimachi chidaonekeranso pamene apolisi mogwirizana ndi khonsolo ya mzinda wa Blantyre adaphwanya ndi kulanda makontena amene anthu amachitiramo bizinesi mumzindawo. Izi zidachitika usiku wa Lolemba ndi Lachiwiri. ",11 "Mwambo odzodza ansembe uchitika ku Blantyre, Zomba By Richard Makombe _0449-1-1024x683.jpg 1024w"" sizes=""(max-width: 662px) 100vw, 662px"" />Mwambo wa malumbiro ngati umenewu uchitika ku Zomba komanso Blantyre Mwambo odzodza madikoni anayi kukhala ansembe mu arkidayosizi ya Blantyre uchitika loweruka ku Limbe Cathedral mu akidayosizi ya Blantyre. Malinga ndi Bambo Alfred Chaima omwe ndi mkulu wa muofesi yoona za utumiki mu arkidayosiziyi ati zonse zokonzekera kudzodza adikoni atatu achibadwiri komanso mmodzi wa chipani cha mzimu woyera tsopano zafika kumapeto. Bambo Chaima ati Ambuye Thomas Luke Msusa ndi omwe adzatsogolere mwambowu. Padakalipano nawo akhristu eni ake ati zokonzekera zizafika kumapeto pomwe magulu omwe akutsogolera miyambo yosiyanasiyana alimbikitsa kukonzekera zochitikazi ngati njira imodzi yokometsa mwambowu. Mmodzi mwa omwe ali mu komiti ya zochitika chitika pa tsikuli Patrick Kombe wati ali ndi chiyembekezo choti akhristu komanso alendo omwe ayitanidwa pa tsikuli azasangalala komanso kuthandiza archdiocese yao pamene ikulandira atumiki atsopanowa. Zonse zili mchimake ndipo pofika tsiku loweruka aliyense yemwe waitanidwa kuti adzabwere mwaunyinji chifukwa mmodzi wa ana awo mu dayosiziyi adzadzodwa pa tsikuli,anatero a Kombe. A Kombe anati ndi kofunika kuti akhristu wa adzaonetse umodzi wawo potenga nawo gawo pa zochitika pa tsikuli pomwe nso dayosizi tsopano yakula ndipo ili ma ma Parish 43. Mu dayosizi ya Zomba mwambo odzodza ma deacon atatu kukhala ansembe uchitikanso loweruka pa pomwenso kukakhale chikondwelero choti ansembe atatu akwanitsa zaka 25 akutumikira mulungu mu diocese ya Zomba. Malinga ndi Bambo Innocent Chiwanda yemwe ndi Pastoral Secretary wa Diocese ya Zomba, Ambuye George Desmond Tambala ndi omwe akatsogolere mwambowu. Ma Deacon atatu wa ndi a Peter Chiopsa, Petro Chilumpha ndi Fortune Gondwe, ndipo ansembe atatu omwe akukondwelera kuti atha zaka 25 akutumikira Mulungu ndi Bambo Daniel Beneti, Bambo Ignancio Bokosi ndi Bambo Charles Namalitha. ",13 " Chakwera angadze ndi kalumo kakuthwa Chakwera (wachiwiri kuchokera ku manja) limodzi ndi mkazi wake Monica komanso akuluakulu ena kumsonkhanowo Mlendo ndiye adza ndi kalumo kakuthwa. Akadaulo pandale ati kusankhidwa kwa mbusa Dr Lazarus Chakwera kukhala mtsogoleri wa chipani chachikulu chotsutsa boma cha MCP kungadzetse kuwala mchipanimo pamene chisankho cha 2014 chili pamphuno. Chakwera adasankhidwa kumsonkhano waukulu wa chipanichi ku Natural Resources College mumzinda wa Lilongwe sabata yatha ndipo ndiye adzaimire chipanichi pa chisankho cha 2014, maso ndi maso ndi mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda yemwe adzaimire chipani cha PP, Peter Mutharika wa DPP komanso Atupele Muluzi wa UDF. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Malinga ndi pulezidenti wa bungwe la akatswiri potambasula za ndale la Political Science Association of Malawi (Psam) Joseph Chunga, kusankhidwa kwa Chakwera kungachititse kuti chithunzithunzi chimene anthu anali nacho pa MCP chisinthe. Iye adanena izi polingalira kuti mbiri ya chipanichi idali ya nkhanza, makamaka paulamuliro wake wa zaka 31 kuchokera mu 1964 pomwe chidathetsa ulamuliro wa atsamunda. Ambiri akukumbukirabe nkhanza za ulamuliro wa MCP umene udachotsedwa mu 1994. Komanso, pakatipa chipanichi chinagawanika chifukwa cha mkangano wa atsogoleri a chipanichi makamaka John Tembo ndi Gwanda Chakuamba. Atangochoka mchipanichi Chakuamba, otsatira ena a chipanichi mchigawo chakumwera adazitulukanso, adatero Chunga. Chakuamba adatenga mpando wa utsogoleri wa chipanichi mu 1997, mtsgoleri wakale wa dziko lino Dr Hastings Kamuzu Banda atausiya chifukwa adali atakula. Iye adaimira chipanichi mu 1999. Koma Tembo adagonjetsa Chakuamba kukovenshoni yokonzekera chisankho cha 2004, ndipo adaimira chipanichi mu 2004 ndi 2009. Chakuamba adatuluka MCP atangogonja kwa Tembo ndipo atsogoleri ena adamutsatira pomwe ena adayambitsa zipani zawo. Chunga adati kudza kwa Chakwera kungachititse kuti kukhale kovuta kuti zipani zina zigonjetse chipanichi chifukwa zipani zambiri zomwe zilipo sizikuonetsa utsogoleri weniweni, makamaka chifukwa anthu amene akutsogolera zipanizo ayesedwa ndipo aunikidwa momwe akuyendetsera ndale. Pajatu kafukufuku wa 2012 Afrobarometer adasonyeza kuti Amalawi 40 mwa 100 alibe chipani makamaka chifukwa chosowa chikhulupiriro mwa atsogoleri andale. Ndiye MCP ikhoza kutolera gawo la anthu amenewa. Koma Chakwera ali ndi ntchito yaikulu yoyanjanitsa komanso kuluzanitsa atsogoleri amene adalephera kupeza mipando, adatero Chunga. Katswiri wa ndale kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, Blessings Chinsinga, wati ngakhale Chakwera ndi mlendo pandale ali ndi mphamvu zodzatengera chipanichi mboma. Iye wati Chakwera atapambana pa chisankhochi, zochitika za mchipanichi ndi zomwe zingamupangitse kuyendetsa bwino dziko kapena kulephera chifukwa cha chilendo chakecho. Ndale ndi zosiyana ndi kayendetsedwe ka bungwe, mpingo kapenanso kampani chifukwa ndale zimafuna kwambiri luso lolimbikitsa maubale lomwe munthu woyamba kumene ndale angavutike kukwaniritsa. Zikutengera zochitika mchipanichi kuti ngati Chakwera atapambana adzalamule dziko bwino kapena ayi. Kumbali imodzi chilendo chake chikhoza kumupangitsa kuti azipanga mfundo zokhwima bwino ndi kuzikwaniritsa posawerengera ndale komanso ngati atamusokoneza ngakhale atapanga nfundo zolimbazo zikhoza kuvuta kuzikwaniritsa kwake, adatero Chinsinga. Chinsinga wati tsopano anthu anayi akuluakulu odzapikisana nawo pampando wa mtsogoleli pa chisankho cha 2014 adziwika ndipo zikuonetsa kuti misonkhano yokopa alendo chaka chino mpakana cha mawa ikhala yovuta kwambiri. Iye wati kutengera anthu anayiwa, zipani zikuyenera kupanga nfundo zamphamvu zodzagulitsira munthu odzaimirirayo chifukwa mpikisano wake udzakhala wa mphamvu. Zikuoneka kuti mpikisano wa chaka cha mawa udzakhala oopsa ndiye mpofunika kupanga mfundo zenizeni osati kutaya nthawi ndi kukamba za munthu kapena zipani zina. Chitukuko chimatengera nfundo zomwe zamangidwa osati kudziwa kulankhula basi, watelo Chinsinga. Katswiriyu wati pamene nyengo ya misonkhano yokopa anthu odzavota yayandikira anthu ayiwale za mipingo, mitundu, ndi malo ochokela koma kumvetsetsa mfundo zomwe zipani zakonzela dziko lino. Ndipo Senior Chief Kaomba ku Kasungu yati kusankhidwa kwa Chakwera ndi chitsimikizo kuti ndale zayamba kukhwima mdziko muno. Iye adati ngakhale Chakwera sadatchukepo mumbiri ya ndale palibe chomuletsa kutsogolera chipani ngati mwini wake akudzidalira komanso ngati wasankhidwa ndi anthu. Timanena za mphanvu ku anthu zimenezi ndiye mphanvu kuanthuzo. Iye ndi munthu wamkulu akudziwa zomwe akuchita chofunika ndi chakuti akuluakulu ena omwe ndi a mkhalakale pandale mchipanimo azimugwira dzanja zonse ziyenda bwino, adatero Kaomba. Chakwera wati kuchokera tsiku lomwe adasankhidwa maso ake ali patsogolo kuwunika mofooka monse kuti adzakonze bwino ngati MCP ingalowe mboma chaka cha mawa. Iye wati ali ndi chikhulupiliro kuti anthu a mchipani cha MCP amuthandiza kuyala mfundo zokomera Amalawi. Chipani cha MCP ndi chachikulu kwambiri ndipo chili ndi ochitsatira ambiri omwe akufuna chitukuko. Kuchipani chathu tikhala pansi bwinobwino ngati anthu okhwima nzeru kuti tione zimene dziko lino likusowa ndikupeza podzayambira kukonza tikadzapambana, adatero Chakwera. Pa zolola amuna kapena akazi kukwatirana okhaokha, iye adauza wailesi ya Zodiak Lachinayi kuti atasankhidwa kutsogolera dziko lino kuti achite zimene Amalawi sakufuna. Ndipo pa za mkangano wa nyanja ya Malawi, iye adati kukambirana ndiye kofunika pakati pa maiko a Malawi ndi Tanzania. ",11 " NRB ionjezera masiku otengera zitupa Ntchito yopereka zitupa za unzika kwa anthu a mmaboma 15 mdziko muno, imene imayenera kutha dzulo ayionjezera mboma la Blantyre, mneneri wa bungwe limene likuyendetsa ntchitoyi watero. Maboma onse a chigawo chapakati komanso Blantyre, Mwanza, Neno, Nsanje ndi Chiradzulu ndiwo akulandira zitupazo mgawo Lachiwiri ndipo malinga ndi mneneri wa bungwe la National Registration Bureau (NRB) Norman Fulatira adati bungwelo laonjezera sabata imodzi kuti anthuwo atenge zitupa zawo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Fulatira Lachinayi adati: Tionjezera sabata imodzi kuti anthu alandire ziphaso zawo ndipo ngati ena akhalebe asadatenge, zitupa zawo akatengera ziphaso zawo ku ofesi ya DC. Fulatira wati amene satenga zitupazo pakutha kwa kuonjezerako azikatengera zitupazo kuofesi ya DC wa boma lawo. Kafukufuku wa Tamvani mumzinda wa Blantyre Lachinayi adavumbulutsa unyinji wa anthu akulimbirana kutenga zitupa ndipo anthu ena amene tidacheza nawo adati ndi bwino ntchitoyi ayionjezere. Patrick Sandramu, yemwe adalembetsa kusukulu ya pulaimale ya Makata ku Ndirande mumzindawo, adati gulu likumakhala kotenga zitupako nchiletso. Kufika lero Lachinayi, anthu ambiri sanatenge zitupa zawo ndipo gulu lake ndi losanena. Ine ndidachita mwayi chifukwa ndimadziwana ndi mmodzi mwa amene akugawa ziphaso ndipo ndidamuuza kuti akachipeza changa andisungire, adatero mkuluyo. Maxwell Majawa Lachinayi adati iye adati adayendera masiku angapo kusukulu ya Zingwangwa kuti atenge chitupa chake. Mbali imene amayendetsa aphunzitsi sizimavuta, koma kumene kumakhala anthu wamba ndiye mavuto analipo. Zoti tizipita kukatenga zitupa motsatira maina athu nazo zidatipomboneza. Ine ndidayendera masiku atatu kuti ndipeze chitupa, adatero Majawa. Ndipo Roselyne Manjawira amene adalembetsa kusukulu ya pulaimale ya Katete ku Chirimba adati pofika Lachinayi adali asanatenge chitupa chake chifukwa cha khamu, komanso chifukwa ameyenera kupita kuntchito. Akadaonjezera masiku chifukwa akanena kuti tizikatengera kwa a DC kukakhala chipwilikiti choopsa kuposa momwe zilili mmaderamu, adatero iye. Izi zili choncho, Madera ena, makamaka amene kulibe anthu ambiri, amatenga mosavuta. Gawoli likatha, lisamukira mboma la Thyolo, Chiradzulu ndi Mulanje. Ndondomeko yopereka ziphasozi idayamba mu October chaka chatha ndipo ikuyembekezereka kutha mu March chaka chino. ",7 "Papa Wasankha Amayi Awiri Mmaudindo Akuluakulu ku Vatican Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wasankha amayi awiri mmaudindo akuluakulu a ku likulu la mpingowu ku Vatican. Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican, Papa wasankha Dr. Rafaella Vincenti kukhala mkulu woyanganira nkhokwe yosungira mabuku yomwe imatchedwa kuti Vatican Apostolic Library ndipo wasankha Professor Antonella Alibrandi kukhala membala wa bungwe lothana ndi mchitidwe wozembetsa ndalama lotchedwa Vatican Financial Information Authority. Malinga ndi likulu la mpingo wa katolika Dr. Vincenti adakhalapo mlembi wa Vatican Apostolic Library pamene Professor Alibrandi ndi membala wa bungwe la maloya mdziko la Italy lotchedwa Milan Bar Association, iyenso ndi President wa bungwe la za chuma ndi aphunzitsi a za malamulo Association of Economics and Law Professors komanso ndi membala wa bungwe la chi Katolika la anthu a za malamulo Union of Catholic Jurists. Nkhokwe yosungira ma buku Vatican Apostolic Library idakhazikitsidwa mchaka cha 1475 ndi Papa Sixto wa 4 ndipo ndi imodzi mwa nkhokwe za kale kwambiri pa dziko la pansi komanso nkhokwe yochititsa chidwi yomwe ili ndi zolembalemba zambiri za mtengo wa patali za make dzana. Ndipobungwe lothana ndi mchitidwe wozembetsa ndalama la Vatican Financial Information Authority adalikhazikitsa ndi Papa Benedicto wa XVIpa 30 December mchaka cha 2010. ",14 "Akhristu Akutsidya La Nyanja Ya Chirwa Akusowa Thandizo Wolemba: Sylvester Kasitomu ent/uploads/2019/09/lake-chilwa.jpg 367w"" sizes=""(max-width: 822px) 100vw, 822px"" /> Akhristu achikatolika ku tsidya kwa nyanja ya Chirwa mu dayosizi ya Zomba apempha anthu akufuna kwabwino kuti awathandize kumalizitsa chalitchi chawo chomwe akumanga. Wapampando wa chalitchi-lii a joseph zakariya ndiwo apereka pemphori pofotokonzera mtolankhani wathu mu mzinda wa Zomba. Malinga ndi a ZAKARIA, ntchito yomanga tchalitchichi yatha ndipo chikusoweka ndi Mbalawala, malata komanso matumba a cement. Kunoko zinthu zambiri ndi zovuta kaamba koti mayendedwe ndi odula timagwiritsa ntchito ku mtunda komanso panyanja kuti tipite kumalo kumene kuli zipangizo zomngira ndiyene anthu attithandiza ndi ndalama ntchito itha kupepukako anatero a zakaria Pamenepa a ZAKARIA ati, akhristu a ku tchalitchi chawo cha St. Peters Ngotakota, amadalira usodzi zomwe akuti ndi zovuta kuti amalizitse ntchito yabwino yomwe yayambika yomanga kachisi wa Ambuye. ",14 " Akati tonde azimveka fungo akutanthauzanji? Miyambi ilipo yosiyanasiyana ndipo ina ukaimva mutu umachita kuwira, kulephera kulumikiza mwambiwo ndi tanthauzo lake. Ena amangoti bola ndanenapo mwambi osalingalira kuti kodi omvera akutengapo phunziro lanji pamwambiwo. Mwambi watitengera pabwaloli lero ndi wakuti tonde azimveka fungo. STEVEN PEMBAMOYO adakumana ndi mfumu Thipwi ya ku Nkhotakota kwa T/A Kanyenda pamsonkhano wokhudza za katetezedwe ka chilengedwe pomwe padatuluka mwambi wozunguawu ndipo adacheza motere: Ndikudziweni, wawa. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Ine ndine Village Headman Thipwi wa mdera la gogochalo Kanyenda mboma lino la Nkhotakota. Pamsonkhano walero mumabwerezabwereza mawu oti tonde azimveka fungo, mumatanthauzanji ndi mauwa? Choyamba mudziwe kuti mawu amene aja ndi mwambi chabe ndiye monga mudziwa mwambi umanenedwa ndi cholinga choti omvera atengepo phunziro kapena chenjezo malingana ndi zomwe zachitika kapena zikuchitika. Nanga poti pamsonkhano umeneuja padali anthu okhaokha padalibe mbuzi? Nchifukwa chake mawuwo akutchedwa kuti mwambi, kutanthauza kuti sakuimira munthu aliyense, ayi, koma kuti pali phunziro lomwe tikufuna kuti anthu atolepo. Mwachitsanzo, msonkhano udali wokhudza za katetezedwe ka chilengedwe pogwiritsa ntchito njira zosiyanasiyana ndiye mwambi umene uja udali woyenerera kuugwiritsa ntchito. Nanga mwambiwu umatanthauzanji? Chabwino, mwambi umenewu umatanthauza kuti ntchito zamanja za munthu ndizo zimamuchitira umboni. Ngati munthu ali wolimbikira, zotsatira za kulimbikira kwakeko zimafotokoza zambiri za iye popanda wina kuima pachulu nkumalalika. Mwachitsanzo, mlimi wolimbikira amadziwika kuti ngolimbikira potengera zokolola zake, chimodzimodzi katswiri wa mpira wosewera kutsogolo amadziwika kaamba komwetsa zigoli. Kutanthauza kuti mbuzi nchitsamba chabe chongobisalirako? Ndi momwemo ndithu, sikuti timatanthauza kuti munthu yemwe tikukambayo ndi tonde poti akumveka fungo la mbuzi, ayi. Iyi ndi njira chabe yoperekera phunziro kapena malangizo ndi chilimbikitso moti apo anthu omwe adali pamsonkhanowu adziwa kuti aliyense pamenepanja azilingidwa ndi zotsatira za ntchito zake, osati kungokamba pakamwa, ayi. Ndiye tonde zikumukhudza bwanji pamenepa, osasankha nyama zina bwanji? Tondeyo ali ndi mbali yake yomwe amagwiritsidwira ntchito. Nkhani yaikulu ndi yakuti mkhola la mbuzi mukamabadwa ana pafupipafupi, ulemu umanka kwa tonde chifukwa ndiye amagwira ntchito mmenemo. Tonde akakhala wolephera kapena kuti ofooka, khola limakhala pomwepomwepo asasuntha, ayi. Ndiye mlimi akaona kuti zaka zikutha mbuzi zake sizikuswana, amakabwerekera tonde wina, uja nkumuchotsamo mwina kumugulitsa kwa mabutchala. Apa ndiye kuti amene uja sadamveke fungo chifukwa tonde mnzakeyo akangolowa mkhola nkuyamba kubereketsa, amalandira matamando kuti ndiye tonde chifukwa zipatso zake zikuoneka. Ndiye kuti aja amati akamva fwemba la munthu nkumati tonde azimveka fungo amalakwitsa? Kwambiri, chifukwa potero paja sipayenera kugwiritsidwa ntchito mwambi umenewu. Atapeza mwambi wina bola monga mwambi wakuti wakumba kanyimbi chifukwa apo zikugwirizana poti kanyimbi naye ali ndi fungo vloboola mmphuno osati masewera, ndiye ngati munthu akumveka fungo losakhala bwino monga mwaneneramo kuti fwemba ndiye kuti akuononga mpweya ndipo anzake akuzunzika ngati momwe amazunzira kanyimbi. ",1 "Anthu Okwiya Apha Bambo Wina Kamba Koba Nyemba Zaziwisi Anthu okwiya mboma la Chikwawa apha bambo wina wa zaka 30 kaamba komuganizira kuti waba nyemba zaziwisi mu dimba la mkulu wina. Malinga ndi wachiwiri kwa mneneri wa apolisi mbomali Sergeant Dickson Matemba, malemuyu Feston Sulupi usiku wa pa 6 July, anapita mmundawu omwe uli mphephete mwa mtsinje wa Shire kukathyola nyembazi koma ali momwemo anthu ozungulira derali anamugwira ndi kuyamba kumumenya. Mbale wawo wa malemuwa anafotokoza kuti mchimwene wawo anapita kukaba nyemba ku madimba omwe ali mphepete mwa mtsinje wa shire ndipo ali kumeneko anthu anayamba kumumenya komwe anakomoka, anatero Matemba. Sergeant Matemba ati anthu ena atamutengera ku chipatala, ndi komwe anakatsimikiza kuti wamwalira. Pamenepa Sergeant Matemba achenjeza anthu kuti asiye kutengera lamulo mmanja mwawo ndipo ati aliyense yemwe wachita izi amangidwa. ",14 " Tsabola ndi waphindu, wophweka kulima Ulimi wa tsabola umaoneka opanda pake komanso ogwetsa mphwayi, koma Benison Kuziona, mkulu wa Bungwe la Zikometso Innovation and Productivity Centre akuti ulimiwu ndi waphindu komanso wophweka. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kuziona adati ndi ndalama yochepa, mlimi amatulutsa ndalama zochuluka. Chaka chathachi, mbewuyi idafika pamtengo wa K3 000 pa kilogalamu ndipo alimi omwe adalima, adachita nayo mphumi kwambiri, adatero mkuluyu. Iye adaonjezanso kuti ubwino wina wa tsabola ndi woti ukabzala chaka choyamba, chaka chachiwiri subzalanso chifukwa mvula ikangogwa mitengo ija imaphukiranso ndipo zokolola zake zimakhala zochuluka kuposa poyamba. Tsabola ndi mbewu imene alimi ena akupindula nayo kwambiri A bungwe la Malawi Fruits mogwirizana ndi Mzuzu Agriculture Development Division (Mzadd) adachita kafukufuku wa tsabola mzaka za mmbuyomu ndipo adapeza kuti kulima tsabola ndi kophweka komanso sikulira ndalama zochuluka poyerekeza ndi mbewu zina. Ngakhale izi zili chomwechi, president wa bungwe la Farmers Union of Malawi, Alfred Kapichira Banda, wati alimi ena atsabola mmadera ena mdziko muno amagulitsa kwa mavenda pamtengo wotsika kwambiri. Iye adati alimi ambiri sakudziwa misika yeniyeni ya tsabola kotero amangoberedwa ndi mavenda. Tikupempha misika yovomerezeka yomwe imagula tsabolayu kuti ibwere poyera, tikufuna alimiwa azitha kugulitsa pa mitengo yabwino, adatero Kapichira Banda. Iye adati chifukwa chakuti alimiwa akhala akugulitsa pa mitengo yotsika, ambiri akumangolima moyerekeza pomwe ena adalekeratu ulimiwu. Bungwe la Zikometso Innovation and Productivity Centre ndi limodzi mwa mabungwe omwe amalimbikitsa za ulimi wa tsabola. Zikometso, ndi nthambi ya bungwe la National Smallholder Farmers Association of Malawi (Nasfam). Ntchito zake ndi kugula tsabola kwa alimi, kuwagulitsa njere zabwino komanso kuwaphunzitsa momwe angalimire tsabolayu kuti azikolola ochuluka komanso wapamwamba. Bungweli lili ndi fakitale yomwe imapanga tsabola wa mmabotolo yemwe amagulitsidwa mMalawi ngakhalenso maiko akunja. Malinga ndi Kuziona, ulimi wa tsabola umayambira ku nazale ngati momwe anthu amachitira ndi ulimi wa mbewu za masamba monga tomato. Tsabola amayenera kufesedwa kumapeto kwa mwezi wa October ndipo akuyenera kuwokeredwa pamene mvula yayamba kugwa yochuluka, adatero Kuziona. Iye adafotokoza kuti mizere imayenera kutalikana masentimita 75 komanso pobzala, mapando amayenera kutalikirana ndi masentimita 45. Akayamba kuphukira, amayenera kudulidwa tisonga take kuti apange nthambi zochuluka. Izi zimathandiza kuti pamtengo uliwonse mlimi adzakolole tsabola ochuluka, adatero Kuziona. Iye adaonjezanso kuti mbewuyi imayenera kuthiridwa feteleza wa D Compound ikangobzalidwa kumene komanso CAN pakadutsa masiku 21. Kathiridwe kake ndi kofanana ndi momwe timathirira ku chimanga. Fetelezayu amathandiza tsabola kuti akule bwino komanso abereke mochuluka, adatero mkuluyu. Iye adaonjezanso kuti tsabolayu nthawi zina amatha kugwidwa ndi matenda komanso tizilombo. Tizilombo tomwe timasakaza mbewuyi ndi tofanana ndi tomwe timagwira mbewu za mtundu wa masamba monga tomato ndipo mankhwala ake ndi ofanana ndi omwe amapoperedwa kumbewuzi. Mlimi akhonza kupopera mankhwala koma chachikulu ndi kubzala mbewu zabwino komanso kumapalira kuti apewe matenda ndi tizilomboti, adatero Kuziona. ",4 " Kusefukira kwa madzi kupha anthu 21 Anthu 21 atsikira kuli chete, pamene ena 100 000 ali kakasi kusowa kopita kutsatira mvula ya mphamvu yomwe yasakaza katundu komanso kusamutsa anthu mdziko muno. Izitu zachitika kuyambira mwezi wa July chaka chatha mpaka mwezi uno wa January. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Malinga ndi nthambi ya boma yoona za ngozi zogwa mwadzidzidzi ya Department of Disaster Management Affairs (Dodma), maboma 24 ndi omwe akhudzidwa ndi mavutowo. Mwa mabomawo, maboma 12 ali mchigawo cha kummwera 8 chigawo chapakati pamene anayi ali mchigawo chakumpoto. Malinga ndi mneneri wa Dodma Chipiliro Khamula, pofika Lamulungu pa 13 January, ngoziyi nkuti itapha anthu 21. Mwa anthuwo, 12 adamwalira ataombedwa ndi mphenzi pamene anthu ovulala pangoziyo adalipo 38, adatero Khamula. Iye adati boma lakhala likuwapatsa anthu okhudzidwawo thandizo monga chakudya, zofunda ndowa ndi zina komanso malo okhala mongoyembekezera. Ntchitoyo ikupitilira ndipo tikadafikirabe madera omwe ma makhonsolo awo atidziwitsa za ngozi, adatero Khamula. Nthambi yoona zakusintha kwa nyengo ya Department of Climate Change and Meteorological Services (Met), yati kuliraku sikutha chifukwa sabata ino mvula yosefula madzi ikatamuka. Ena mwa maboma okhudzidwa ndi Nsanje, Karonga, Mulanje, Chikwawa, Balaka ndi Lilongwe. Polankhula ndi Tamvani, DC wa boma la Mulanje, Charles Makanga adati madzi osefukira ochokera mumtsinje wa Thuchira, Lolemba pa 14 adaononga minda ya anthu 520 ochokera mmidzi ya Kada ndi Nongwe kwa mfumu yaikulu Nkanda. Apapa ndiye kuti anthuwo akufunikira thandizo la mbewu ndi zofunikira zina chifukwa minda yawo yakokoloka, adalongosola Makanga. Iye adatinso anthu 680 mdera lina komweko ali kakasi mvula ya mphepo itasakaza nyumba zawo. Tikuyesetsa kupereka thandizo loyenera kwa anthuwo ngakhale tikudikirabe thandizo lofika kwa anthu omwe ali kakasi ochokera kumsika wa njala komwenso mvula ya mphepo idasakaza katundu, adalongosola Makanga. Sabata yathayo, anthu awiri adamwalira mboma la Balaka ndi wina mboma la Mangochi chipupa cha nyumba yawo chitawagwera kutsatira mvula yomwe idagwa mmabomawo. Ku Mzimba kwa Mberwa, Jalavikuwa, Ntwalo ndi Mabulabo mabanja pafupifupi 1000 akhudziwa ndi mvula ya matalala komanso madzi osefukira. DC wa bomalo, Thomas Chirwa adati chifukwa choti madera ambiri akhudzidwa pakamodzi, anthu ambiri sadalandirebe thandizo. Mzinda wa Lilongwe ndi malo enanso omwe madzi adazunguza sabata yatha. Anthu 176 adasamutsidwa ndi madzi ndipo katundu adaonongeka. Nduna ya zachitetezo mdziko muno yomwe yakhala ikuyendera anthu okhudzidwawo, Nicholus Dausi idati ngozizo zanyanya chaka chino ndipo mpofunika kuti anthu akhale osamalitsa kukamagwa mvula kapena mphepo. ",5 "Amayi Okhudzidwa Akuyembekezeka Kuchita Ziwonetsero Poteteza Ansah By Thokozani Chapola Amayi omwe akuti ndi okudzidwa ndi ziwonetsero zokakamiza wapampando wa bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) mayi Jane Ansah kuti atule pansi udindo wake, alengeza kuti achita ziwonetsero mu mzinda wa Blantyre mawa lino. White kulira pa msonkhano wa atolankhani pomwe amalengeza za ziwonetserozi Iwo alengeza izi pa msonkhano wa atolankhani womwe anachititsa lolemba mu mzinda wa Blantyre. Mmodzi mwa amayiwa yemwenso ndi wapampando wa bungwe lomwe akulitcha Concerned Women a Seodi White wati ndi zokhumudwitsa kuti mayi Jane Ansah akutonzedwa ndi kunyazitsidwa mu njira zosiyanasiyana kaamba koti anali wapampando wa bungwe lomwe limayendetsa chisankho chapatatu. Iye wati akukhulupilira kuti anthu akuchita izi powona kuti mayi Ansah ndi munthu wamayi. Kuyenda kumeneku tikufuna kusonyeza kuti ife tili pambuyo pa mayi Ansah. Chisankho cha 2014 munthu mpaka anafa koma anthu sanapange ziwonetsero chifukwa anali munthu wammuna pano ndiye palibe munthu amene wafapo pa chisankhochi koma ena akupanga ziwonetsero. Ife tikuwona kuti anthu akupanga zimenezi chifukwa ndi mzimayi, anatero mayi White. Padakali pano nduna yowona za kusasiyana pakati pa amayi ndi abambo mayi Mary Navitcha ati akachita nawo ziwonetserozi Koma polankhulapo mmodzi mwa akatswiri pa nkhani za ndale mdziko muno a Enerst Thindwa ati ndi zodabwitsa kuti anthu omwe ali patsogolo kuchita izi ndi a chipani cha DPP komanso ena ali ndi maudindo mu nthambi za boma komanso ena ndi omwe anali patsogolo kunyoza ulamuliro wa mtsogoleri wakale wa dziko lino mayi Joyce Banda yemwenso ndi munthu wa mayi zomwe ati zikusonyezeratu kuti anthuwa akupanga zofuna zawo osati za a Malawi. Gulu limeneli ambiri ndi achipani cha DPP ndiye zikudabwitsa kuti dpp ndi nkhani ya chisankho zikugwirizana bwanji. Enanso mwa amenewa ndi amene amakhala patsogolo kunyoza amayi anzawo. Kumbukirani nthawi ya Joyce Banda mmodzi mwa amayi amenewa ndi amene anali patsogolo kunyoza mayi Banda ndiye lero zikudabwitsa kuti abwera ndi ganizoli, anatero a Thindwa Komabe a Thindwa ati ndi koyenera kuti amayiwa apatsidwe mpata wochita ziwonetserozo kaamba koti ndi ufulu wawo kutero malinga ndi malamulo a dziko lino. ",11 " Njala yavuta, mafumu achenjeza Mafumu ena mdziko muno apempha boma kuti liwathandize kuthana ndi njala yomwe yayamba kale kusautsa maboma angapo ndipo madera ena ayamba kale kupulumukira zikhawo. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mafumuwa ndi T/A Kachindamoto ku Dedza, Tengani ku Nsanje ndi Mlauli ku Neno. Izi zikudza patangodutsa sabata ziwiri a bungwe lounikira ndi kuchenjeza za njala la Famine and Early Warning Systems Network (Fewsnet) litachenjeza kuti pafupifupi anthu 1.7 miliyoni asowa chakudya mdziko muno chaka chino. Lipoti la bungweli linaunikira za kapezekedwe ka chakudya mdziko muno kuyambira mwezi wa Ogasiti chaka chino mpaka Malichi chaka cha mawa. Kuunikiraku kunatinso ntchito zolimbana ndi njalayi zikuoneka kuti nzosakwanira kwenikweni ndipo zingakhale zitagugiratu pofika Novembala kapena Disembala chaka chino. Poonjezera, zounikirazi zinati mwa maboma okhudzidwa ndi Nsanje, Chikhwawa, Balaka, Blantyre, Phalombe, Machinga, Zomba, Thyolo, Mulanje, Neno, Mwanza, komanso Mangochi ku chigwawo cha kummwera, Salima ndi Ntcheu pakati komanso mbali zina mdera la kumpoto mboma la Karonga kumpoto. T/A Kachindamoto wati kumeneko midzi 300 yomwe muli anthu pafupifupi 70 000 yakhudzidwa ndi njalayo. Tidali ndi msonkhano ndi a bungwe la zaulimi ndipo tidapeza kuti tikufunika [thandizo la] matani 1 000 a chimanga. Tidayesera ulimi wa mthirira koma zakanika chifukwa mitsinje yaphwa. Ngati sitingalandire thandizo mpaka Disembala, chiyembekezo chilipo kuti anthu ataya miyoyo, yatero mfumuyo. Kachindamoto wati njalayi yagwa kaamba kosowekera mvula mmadera angapo komanso kuchuluka kwa mvula mmadera ena. Tidabzala kawiri kaamba ka vuto la mvula koma sizidaphule kanthu.Kumapeto nkomwe kudabwera mvula yambiri mpaka madzi kusefukira, adatero Kachindamoto. T/A Tengani wati galu wakuda sadasiye malo pomwe anthu 20 000 pansi pake akhudzidwa ndi njalayi. Vuto kumeneko akuti lidali lakusowa kwa mvula. Tidafika potopa kulankhula za njala kuno.Boma litithandize ndi zipangizo kuti tiyambe ulimi wa mthirira chifukwa pafupifupi dera lililonse kuno lakhudzidwa ndi njala, idatero mfumuyi yomwe yati dera lake lili ndi anthu pafupifupi 35 000. Iye wati posakhalitsapa ena ayamba kudya nyika chifukwa chosowa pogwira. Tengani adati madera ena kumeneko ayamba kale kulandira ufa ndi thandizo lachimanga. T/A Mlauli wati ku Neno mvula siidagwe bwino ndipo njala yakhudza pafupifupi boma lonse.Mlauli wati mmudzi mwake muli anthu 25 903 ndipo pafupifupi onse akhudzidwa ndi njalayo. Tikufuna thandizo mwachangu, adatero Mlauli. Mkulu wa bungwe loona za ndondomeko za ulimi lomwe si laboma la Civil Society Agriculture Network (Cisanet), Tamani Nkhono-Mvula, wati alandilapo malipoti kuti mabomawa akhudzidwa ndi njala. Iye wati kotero boma likuyenera kuvomereza kuti mdziko muno muli njala ncholinga choti mabungwe ayambe kuthandiza. Iye adati mabungwe ali chile kuthandiza anthu koma pena amadikira boma livomereze za vuto lomwe lagwalo. Pena atsogoleri amatha kuvomereza kapena kukana kuti kulibe njala pazifukwa za ndale ndipo mabungwe amakhala omangika kuyamba kuthandizapo. Chakudya mdziko muno chilipo. Chiyembekezo chilipo kuti anthuwa apulumutsidwa, adatero mkuluyu. Koma mneneri wa boma, Moses Kunkuyu, wati boma layamba kale kugawa chakudya mmadera ena omwe akhudzidwa ndi njalayi kotero madera omwe sadalandire thandizoli akuyenera kudziwitsa boma. Iye wati msabatayi madera ena okhudzidwa ndi njalayi mboma la Blantyre ndi amene amalandira thandizoli. Malinga ndi unduna wa zamalimidwe, dziko lino lidakolola matani 3.6 miliyoni a chimanga pomwe dziko lino limafunika matani 2.8. Chiyambire malipoti a njalawa, bola lakhala likutsutsa, ati dziko lino lili ndi chakudya chokwanira. Mmbuyomu, Nduna ya Mapulani a Chuma ndi Chitukuko, Atupele Muluzi, inati kuunikira kwa Fewsnet kunali kosadalirika, ati mdziko muno muli ndondomeko yomwe ingadziwe bwino za chiwerengero chomwe chili pa chiopsezo cha njala. Mu Julaye chaka chino, ndondomekoyo inati anthu 1.63 miliyoni ndi omwe anali pa chiopsezo. Chiopsezochi chikudza pomwe dziko lino likukumbukira tsiku lachakudya padziko lapansi, tsiku lomwe limakumbukukiridwa ndi mayiko oposa 150. Tsikuli lomwe limakumbukiridwa pa 16 Okutobala likukumbukiridwa pamutu woti Mgwirizano wa mabungwe azaulimi; ngodya yodyetsera dziko. ",8 " Mavuto a UDF angaphe demokalase Chipasupasu cha mchipani chakale cholamula cha United Democratic Front (UDF) chingaopseze ulamuliro wa demokalase mdziko muno womwe umalira kuti pakhale zipani zotsutsa zamphamvu zothandiza kuongolera pomwe chipani cholamula chikulakwitsa. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Katswiri wa phunziro la ndale kudzanso otumikiridwa pandale aikira ndemangayi potsatira mgwedegwede womwe wakula mu chipani cha UDF. Iwo ati kufooka kwa UDFchimodzimodzi mikangano ya mchipani china chotsutsa chachikulu cha MCPkupereka mwayi kwa chipani cholamula cha DPP kuyenda moyera, mosatsutsidwa pa maganizo a kayendetsedwe ka boma. Katswiri pa maphunziro a ndale yemwenso ndi mphunzitsi pa sukulu ya ukachenjede ya Mzuzu, Noel Mbowela, wati chipani cha UDF chidali cha mphamvu polingalira kuti chidalamulapo koma awa ndi malecheleche ngati sichikonza zolakwikazi. Iye adati ngati zipani zotsutsa zili za mphamvu, zimakakamiza chipani cholamula kuti chidzilabadira zofuna za anthu ndipo izi zimapindulira dziko. Kuunikiraku kwadza pomwe tsopano mamulumuzana a UDF, omwe ena mwa iwo ndi a komiti yaikulu yachipanichi, agawikana ndipo kuli mbali ziwiri zomwe sizionana ndi diso labwino. Mbali imodzi kuli Gorge nga Ntafu, mlembi wamkulu Kennedy Makwangala, Lilian Patel, Atupele Muluzi komanso aphungu onse 15 a chipanichi ku Nyumba ya Malamulo. Mbali ina kuli Friday Jumbe yemwe adapatsidwa ulamuliro wachipani ndi wapampando wakale Bakili Muluzi, Hophmally Makande, Sam Mpasu, Humphrey Mvula komanso Ken Nsonda. Pano mbali ya Jumbe yalengeza kuti yachotsa Makwangwala komanso Atupele pomwe ati awiriwa adalephera kukaonekera ku komiti yosungitsa mwambo yachipanichi. Koma Msonda wati anthu asadandaule chifukwa zomwe zikuchitikazi pochotsa ena ndi njira imodzi yokonzera chipanichi. Iye wati mavuto onse omwe ali kuchipanichi adadza ndi Bakili chifukwa chodzitengera mwa yekha zochitika mchipanimo. Mgwedegwede mchipanichi udakula mwezi wa Okutobala 2011 pomwe Atupele Muluzi adabwera poyera ndikulengeza khumbo lake lodzaima nawo pa mpando wa pulezidenti mchaka cha 2014. Izi sizidakomere komiti yaikulu mchipanichi yomwe idati izi ndizosemphana ndi malamulo achipanichi. Apa chipanichi chidaitanitsa Atupele kuti akaonekere ku komiti yosungitsa mwambo yachipanichi koma iye adakana ndipo komitiyi idalengeza kuti yamuchotsa mchipani. Msonda wati aphungu onse akunyumba ya malamulo ali mbali ya Atupele, yemwenso ndi phungu wa dera la kumpoto cha kummawa kwa Machinga. Kugwedezekaku kudakulanso pa 21 Disembala 2011 pomwe Makwangwala adatulutsa kalata yomwe Msonda wati nkutheka idalembedwa atanamizidwa ndi Bakili Muluzi. Kalatayo idati: Maudindo onse a mchipanichi abwerera momwe adaliri pa 16 Julaye 2009 pomwe wapampando wachipanichi, Bakili Muluzi adanyamuka kupita kuchipatala ku UK ndikusiya zonse mmanja mwa mlembi wa mkulu wachipanichi. Ngodya zomwe zakonzedwa kuchoka pa 16 Julaye 2009 zonse zamasulidwa ndipo mamembala onse achipanichi omwe adakakamizidwa kuchoka mchipanichi abwezeretsedwa pamaudindo awo. Msonkhano wa komiti yaikulu yachipani udzachitika ku likulu la chipanichi ku Limbe pa 28 Disembala 2011 nthawi ya 9 koloko mmawa. Apa mamulumuzana ena achipanichi komanso Msonda adati kalatayo yalembedwa mosafunsa akuluakulu achipanichi. Iwo adati Makwangwala alibe mphamvu zoterezi chifukwa komiti yomwe ikugwira ntchito ndiyo idayenera kubweretsa poyera mfundozi ku komiti yaikulu ya chipani zisanatuluke. Msonda wati mfundo zomwe zidalembedwa mkalatayo, zikutanthauza kuti Bakili Muluzi ndiye adabweretsa mfundozi kuti Makwangwala alembe. Pa 16 pomwe akunenapo, Muluzi adatula maudindo kwa komiti yomwe ikugwira ntchito ndipo maudindowa adawatenganso atabwera kuchoka kuchipatala. Mu Disembala 2009, Muluzi adatulira udindo Jumbe pomwe adalengezanso kuti akusiya ndale. Lero wina akamati maudindo onse abwerera mwakale, akutanthauza kuti Muluzi wayambiranso ndale? Apa ife tikutsimikizirika kuti zonsezi akuchita ndi Muluzi, adatero Msonda. Kalatayi itangotuluka, akuluakulu achipanichi pamodzi ndi Msonda adakatenga chiletso choletsa msonkhano wa pa 28 Disembala. Chipanichi chidaitanitsa Makwangwala komanso Atupele ku komiti yosungitsa mwambo, koma awiriwa sadatuyukire. Apa awiriwa adachotsedwa mchipanimo nkusankha Hophmally Makande kuti akhale wogwirizira mpando wa mlembi wachipanichi. Chipanichi pa 27 Disembala chidaitanitsa Bakili Muluzi kuti akaonekere ku komiti yosungitsa mwambo pa 11 Januwale 2012 koma Muluzi, pobwera kuchokera ku Zambia, adati izi nzamkutu. Kalata yomwe idalembedwa ndi Makande idati Muluzi akuyenera kukayankha milandu itatu. Iyi ndiyo kusowetsa K125 miliyoni yachipanichi, kutenga katundu wachipani ndikukamulembetsa mdzina lake komanso kuitanitsa mamembala achipanichi pamodzi ndi Makwangwala pa 21 Disembala ku zokambirana chikhalilecho alibe mphamvu zotere malinga ndi gawo 12 (b)(vi), 12(b)(vii) ndi 12(b)(ix) a malamulo achipanichi. Mbowela wati zonsezi zikuonetsa kuti chipanichi komanso ulamuliro wa zipani zambiri ukulowera kuchiwonongeko. Sam Banda wa mmudzi mwa Chipoka kwa T/A Mponda mboma la Mangochi wati chipasupasuchi chikusokoneza anthu: Nditsate ziti? Sitikudziwa kuti tidzavotera ndani. Akuyenera kugwirizana zochita, adatero Banda. Sanudi Tambula wa mmudzi mwa Kalembo kwa T/A Kalembo mboma la Balaka wati chidwi ndi chipanichi chikuchoka. Msonda waloza chala Bakili Muluzi ndipo wakumbutsira zomwe adachita Muluzi ati potenga munthu wakunja kwa chipaniBingu wa Mutharikandikumupatsa ulamuliro wa UDF pa chisankho cha 2004. Iye adati pano Muluzi wayamba kugwiritsa ntchito ena monga Makwangwala kuti azibweretsa zachilendo mchipanichi, zomwe komiti yaikulu ikukana. Mchaka cha 1994 pomwe chipanichi chidalowa mboma, chipanichi chidali ndi aphungu 92 mnyumba ya malamulo ndipo pofika 1999 nkuti chili ndi aphungu oposa 100 chifukwa aphungu a chipani cha Alliance for Democracy (AFORD) adagwirizana ndi chipanichi. Mchaka cha 1999 mpaka 2004 chipanichi chidali ndi aphungu 55 ndipo panthawiyi chipani cha MCP ndicho chidatenga aphungu ambiri. Pano chipanichi chili ndi aphungu 15 okha kunyumba ya malamulo. ",11 " Amatsutsanabe zamakumanidwe awo Ambiri akapezana nkukondana nkugwirizana za banja amakhala ndi chikumbumtima cha komwe ndi mmene adakumanirana, koma ndi nkhani yochititsa chidwi kumva za Chiyembekezo Focus Maganga ndi Lydia Kalonde. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Awiriwa akuti mpaka lero sagwirizanabe za malo ndi tsiku lomwe adakumana koyamba ndipo chomwe amakumbukirako nchakuti mudali mchaka cha 2013 ndipo adapanga chinkhoswe pa 7 June 2013. Chomwe ndimakumbuka ine nchakuti ndidakamupeza kuofesi yake nditapita ndi mnzanga Dickson Kashoti pomwe iye amakakamira kuti tidakumana koyamba mminibasi koma kwa ine uku kudali kukumana kwachiwiri, adatero Focus. Focus ndi Linda pachinkhoswe chawo Panthawiyo nkuti Focus akugwira ntchito ya utolankhani pomwe Lydia adali wothandizira mkulu wa zofalitsa mawu kuunduna wa zofalitsa mawu komwe ali mpaka pano. Focus adati poti awiriwa alibe tsiku lokhazikika lomwe angati adakumana koyamba, chomwe amakumbukira nchakuti atakumana kuofesi ya Lydia adangopatsana moni polingalira kuti idali nthawi ya ntchito. Kwinaku akuti amakumbukira kuti atakumana mminibasi Lydia adali ndi chidwi ndi momwe iye adavalira, suti yapamwamba koma tsitsi losapesa ndipo mmaganizo mwake amangoti mwina wadzuka ndi mowa mmutu. Ngakhale adali ndi maganizo oterewa, macheza adayenda bwino mpaka posiyana tidapatsana nambala za foni nkumaimbirana mwakathithi mpaka chibwenzi chidayamba, adatero Focus. Iye adati chitachitika chinkhoswe iwo adalowana asadapange ukwati pofuna kukonzekera mofatsa ndipo akuti ukwatiwo ukhalako kumapeto kwa chaka chino. Focus akuti amakonda kwambiri Lydia chifukwa ndi wooneka bwino, wanzeru, wachikondi, woopa Mulungu komanso amamuthandiza nzeru ndi kumulimbikitsa akamafooka. Naye Lydia akuti amamukonda kwambiri Focus kaamba ka zochitika zake komanso masomphenya ndi kulimbikira pochita zinthu. Amapanga zondisangalatsa komanso ali ndi khama ndi luntha pochita zinthu. Tidapezana okonda kupemphera tokhatokha komanso ansangala, adatero Lydia. ",15 " Bwanji nkhuku yoweta sagula pamsika? Achewa ali ndi njira zosiyanasiyana zoperekera malango pakati pawo. Njira zina ndi monga nthano, magule, ndakatulo, chinamwali ndi miyambi ndi zininga. Lero nkhani yathu yagona pa miyambi ndipo tifukula mwambi wakuti nkhuku yoweta sagula pamsika. STEVEN PEMABMOYO adacheza ndi mfumu yaikulu Njewa ya ku Lilongwe, yomwe ikutambasula za mwambiwu. Choyamba, mfumu, tafotokozani za momwe nkhani ya chikhalidwe cha makolo ilili kuno. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kwathu kuno ndi dera limodzi lomwe anthu sataya chikhalidwe cha makolo ndipo kuti mukhale pakati pathu kwa masiku angapo mukhoza kuona kusintha poyerekeza ndi zomwe mudazolowera kuona. Anthu a kuno adamva mwambo ndipo adausunga. Njewa kufotokoza za tanthauzo la mwambiwo Tsono mukati adamva mwambo mukufuna kunena kuti adaumva bwanji? Pakati pa Achewa, mwambo ndi chuma chosiyirana. Makolo kalero adasiyira ana awo omwe adasiyiranso ana awo chonchoo mpakana lero timangosiyirana kuti mpakana kalekale mtundu wathu usadzasokonekere ayi. Ndikufuna kudziwa kusiyiranako mumachita kupatsana pamanja? Ayi, mwambo si chithu choti mungachione kapena kuchigwira. Imakwana nthawi yoti makolo amadziwa kuti mwana uyu akufunika kudziwa zakuti ndiye amakonza njira yomupatsira mwambo womwe ukufunikawo. Pali njira zingapo monga kutengera mwana kutsimba, kudambwe, kumuitanira anamkungwi kapena kudzera mmiyambi yomwe amatolamo tanthauzo. Eya pamenepo, pali mwambi uja amati nkhuku yoweta sagula pamsika. Mwambi umenewu uli ndi tanthauzo ndithu? Kwabasi, mwambi umene uja uli ndi tanthauzo lozama kwambiri ndipo mwachita bwino kusankha mwambi umenewu chifukwa umakhudzana ndi moyo wa munthu, makamaka akakula, kuti akukalowa mbanja nkukayamba moyo wina. Ndikufuna mumasule bwinobwino kuti nkhuku ikubweramo bwanji. Chabwino, ndiyambe ndi kumasulira motere: munthu ukafuna nkhuku yoti uwete, supita pamsika chifukwa akhoza kukugulitsa yodzimwera mazira kapena yoti idatopa kale kuikira ndiye kuti palibe chomwe wachitapo. Pokagula nkhuku yoweta umafika pakhomo pomwe pali khola ndipo umafunsa umboni woti nkhukuyo ikadaikira kapena isadayambe nkomwe ndipo kuti mtundu wake umaikira motani. Apa zimatanthauza kuti munthu akafuna banja sangangopita pamsewu nkutengana ndi mkazi kapena mwamuna osadziwa mbiri yake, komwe amachokera ndi mtima wake. Koma amayenera kutani? Munthu wanzeru amayenera kupita kwa makolo kapena abale a munthu yemwe wamukonda kukaonako ndi kuphunzira khalidwe lawo. Akhozanso kufufuza kudzera kwa anthu adera omwe amakhala kufupi ndi munthuyo, akakhutira akhoza kuyambapo dongosolo. Izi ndi zomwe makolo amatanthauza mmwambiwu. Paliso pena pomwe mwambiwu ungagwire ntchito? Kwinako zikhoza kutengera kuti pali nkhani yanji koma bola tanthauzo lake likhale loti pakufunika kusamala, makamaka kuchita kafukufuku osangophwanyirira pochita zinthu. Koma gwero lenileni makolowo poyambitsa mwambiwu adayambitsira nkhani ya maukwati. ",10 " Kuli ziii! Pa za mthandizi Kwangoti zii! Nkhawa yagunda ngati ntchito za mthandizi zomwe anthu amalandira kangachepe akalima msewu ichitike popeza nthawi yake yadutsa osamvapo kanthu. Iyi ndi ndondomeko yomwe anthu amalima misewu ndi kulandira ndalama yomwe imathandiza nthawi ya njala. Chaka chilichonse ntchitoyi imachitika mu January ndi February. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Koma pano miyezi itatu yatha mwachinunu, osamva kanthu kuchokera kuboma. Izi zadabwitsa mafumu amene amakhudzidwa ndi ntchitoyi pomemeza anthu a mmidzi yawo kuti akalambule misewu. Mfumu Kabunduli ya mboma la Nkhata Bay yati njala ikukuta anthu a mdera lake amene amapindula ndi ntchitozo. February ndi mwezi wa njala, chaka chino anthu akutuwa ndi njala chifukwa cha ngamba. Timadalira kuti tipezako mpumulo tikayamba kulima misewu koma mpaka lero, idatero mfumuyo. Koma mkulu woona momwe ntchito zachitukuko zikuyendera kunthambi ya Local Development Fund (LDF), Booker Matemvu, wati ntchitoyi yasintha kusiyana ndi zaka zonse. Ntchitoyi iyamba mu September ndipo idzatha November chaka chino. Iyi ndi nthawi yomwe takonza kuti anthu adzayambe kulima misewu, adatero Matemvu. Ganizoli likudabwitsa Kabunduli. Asinthiranji? Kapena zalowa ndale? Chifukwa mwezi wa njala ndi February mpaka March. Apapa ndiye kuti asokonezeratu cholinga cha ndondomekoyi, adatero iye. Tili ndi anthu kumudzi amene alibe chilichonse, ganyu ndi wovuta kumupeza ndipo amadalira kulima misewu kuti apeze thandizo. Popezera ndalama ndi ntchito yomweyi, ndiye akusinthanso? Matemvu wati kusinthaku kwachitika chifukwa zimatenga nthawi yaitali kuti anthu alandire ndalama zawo akalima misewu mu February. Pena zimafika April anthu asadalandire, nchifukwa chake tasintha. Komanso dziwani kuti mmidzimo tayambitsa ntchito zina zomwe anthu akugwira polandirapo ndalama monga kubwezeretsa zachilengedwe, adatero Matemvu. Iye adati akukambirana ndi boma kuti ndondomekoyi ichitike monga imachitikira zaka zonse chifukwa cha anthu amene akutuwa ndi njala. Talandira madandaulo kwa anthu, maka a mmadera amene akhudzidwa ndi njala. Ngati zonse zingathe bwino ndiye kuti ntchitoyi itha kuyamba nthawi iliyonse September asadafike, adatero Matemvu. Ngakhale ntchitoyi idzayambe mu September monga momwe Matemvu akunenera, madera ambiri misewu ndi yoonongeka chifukwa cha mvula pamene ina ndi yosalambulidwa. Ndalama zolimitsira misewuyi zachoka ku World Bank. Nthambi ya LDF yomwe imayendetsa ndondomekoyi idalandira kale K97 biliyoni (132 miliyoni dollars) kuti zigwire ntchito mpaka chaka chamawa. Njala yakhudza maboma a Neno, Nsanje, Chikwawa, Balaka, Mwanza, Phalombwe, Ntcheu, Blantyre, Karonga ndi ena. ",15 "Matenda Osapatsirana Akuchuluka-Boma Wolemba: Sylvester Kasitomu Boma kudzera muunduna wa zaumoyo lati pofika mchaka cha 2025 anthu ambiri mdziko muno azakhala atakhudzidwa ndi matenda monga kuthamanga kwa magazi ndi shuga kuposa matenda opatsirana monga a Edzi. Mkulu othandizira kuyendetsa zipatala ku matenda asapatsirana mdziko muno ku undunawu a Hestings Chigalu Chiumia ndiwo ayankhula izi mboma la zomba pomwe amafotokozera akuluakulu aboma la zomba za matenda amgonagona osapatsirana-wa. Mwazina a Chiumia alangiza anthu kuti apewe kusuta fodya ndi kuledzara alimbikitse kudya zakudya zamagulu komanso kuchita masewera olimbitsa thupi zomwe ndizothandiza kuti asadwale matendawa. Mwazina iwo anati anthu ambiri ngati sasata njira zoyenera pakayendetsedwe kwa moyo wawo azadwala matendawa kuposa amene azapezeke ndi matenda opatsilana monga edzi malungo ndi zina. Tikamafika mu chaka cha 2025 anthu ambili azakhala atadwala matendawa kaamba koti anthu masiku ano akukonda kudya zakudya za nyama chipisi cha pachiwaya ndi zina zomwe zingapangitse kuti chiwerengero cha mafuta amthupi chikwere ndikuamba kudwala matendawa, anatero a Chiumia. Mwazina iye wapepha anthu kuti apewe kudya zakudya zomwe zingakoledzere kukwera kwa chiwerengero cha mafuta mthupi komanso kukonda kuchita masewera kafukufuku anasonyeza kuti muchaka cha 2009 anthu odwala matendawa anali 33 pa hundred aliwonse odwala matenda a bp ndipo 6 pa hundred aliwonse odwala matensda a shuga ndipo mu chaka cha 2016 chinafika kufika pa 19 pa hundred aliwonse odwala bp ndipo atatu pa hundred aliwonse odwala shuga. ",6 "Anjata anthu 21 Kamba Kotentha Polisi ya Malomo Apolisi mboma la Ntchisi amanga anthu 21 powaganizira kuti akukhudzidwa ndi kuwotchedwa kwa polisi ya Malomo mbomalo. Wofalitsa nkhani za apolisi mbomalo Sub Inspector Richard Kaponda watsimikiza za nkhaniyi polankhula ndi Radio Maria Malawi. Iye wati mwa anthuwa, asanu ndi amayi pamene 16 ndi abambo, ndipo onsewa akuyembekezeka kukayankha mlandu wotentha nyumba ya boma zomwe ndi zotsutsana ndi gawo 337 la malamulo oyendetsera dziko lino. Sabata ziwiri zapitazo, anthuwa anagwira munthu wina yemwe amamuganizira kuti ndi opopa magazi ndipo mmene apolisi amafuna kulesetsa mkuluyo pamene amafuna kutenthedwa ndi gululo, ndi pomwe anthuwo anayamba kugenda ndi kutentha polisiyo. Kaponda wachenjezanso anthu omwe akufalitsa mbiri yoti mdziko muno muli opopa magazi kuti akapezeka adzayimbidwa mlandu Kamba koti limeneli ndi bodza la mkunkhuniza. ",7 "NASME Yapempha Amayi Achilimike Pamalonda Bungwe la business zingono-zingono la National Association of Small Business and Medium Enterprises NASME lachinayi lalimbikitsa amayi kuti achilimike komanso kutsata njira zovomerezeka zochitira malonda awo. Mmodzi mwa akuluakulu ku bungweli a Charles Nyekanyeka ndi omwe anena izi lachinayi ku Maula Cathedral mu mzinda wa Lilongwe pa maphunziro a tsiku limodzi okhudza momwe amayi angapititsire patsogolo malonda awo. Iwo ati ochita business zingono-zingono akuyenera kutsatira bwino njira zoyenera zovomerezeka ngati akufuna kugulitsa katundu wawo ku maiko akunja ngati njira imodzi yopititsira patsogolo malonda awo. Kwakukulu bungwe lathu likugwira ntchito ndi amayi omwe amachita ma bizinezi osiyanasiyana kuti abwewre pamodzi ndikuphunzitsana ma upangiri amene angachitire mabizinezi awo antero nyekanyeka. Polankhulapo mmodzi mwa amayi ochita malondawa, mayi Doreen Mtawi ati kudzera mu bungwe la nasme amayi wa apeza maupangiri abwino omwe angachitire mabizinezi awo monga kudziwa misika yoyenera ya zokolora zawo komanso kugulitsa zokolorazi pa mitengo yabwino zomwe zawapezetsa phindu lokwanira. Kukhala mmaguru ndi kothandiza kwambiri kaamba koti umapeza zinthu zoti pa iwe wekha siungazipeze monga kupeza misika ya zokolora ndi zina zambiri antero mayi Mtawi. Bungwe la NASME linakhazikitsidwa ndi cholinga chofuna kuti liziyanganira mabungwe angonoangono pomwe mwazina limathandiza amayi ochita malonda kuwapezera misika ya malonda awo yovomerezeka. ",2 " Zipani zigonjera chiletso cha Escom Chipani cha MCP chati chichotsa mbendera pamapolo Zipani za ndale mdziko muno zagwirizana ndi chiletso cha bungwe loyendetsa ntchito za magetsi mdziko muno la Escom choti zipani zandale zisamapachike mbendera zawo pazipangizo zake monga mapolo a magetsi. Mneneri wa chipani cha MCP Jessie Kabwila wati bungwe la Escom ndi lolandiridwa paganizo lakeli, koma wapempha kuti bungweli litsate njira zabwino pochotsa mbenderazo kuopa kuononga. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC A Escom sakulakwitsa chifukwa akuganizira za chitetezo cha anthu, koma tingopempha kuti pakhale kulumikizana kwabwino kuti katundu wathuyu asaonongeke poti ndi wodula, adatero Kabwila. Mlembi wamkulu wa chipani cha PP Wakuda Kamanga naye wati palibe cholakwika bungwe la Escom kuchita izi chifukwa ngozi za magetsi zimaopsa, makamaka ngati anthu akuseweretsa zida za magetsi. Iyi ndi njira imodzi yomwe bungwe la Escom laona kuti ikhoza kuthandiza kuchepetsa ngozi komanso kuteteza katundu wawo, choncho ife tikambirana ndi achinyamata athu kuti akachotse mbendera zomwe zili pamapolo a magetsi, adatero Kamanga. Koma mneneri wa chipani cha DPP Nicholas Dausi adati chipani chawo sichipachika mbendera zawo mmapolo a magetsi. Zimenezo mukafunse a PP, ife sitiika mbendera pamapolo a magetsi, adatero Dausi Tamvani itamufunsa za maganizo a chipani chake pa chiletso cha bungwe la Escom. Wachiwiri kwa mneneri wa bungwe la Escom George Mituka wati bungweli lidayamba kuganiza za nkhaniyi kalekale ndipo lakhala likukambirana ndi makampani ndi makhonsolo pa chimene angachite. Mituka adati aganiza zochita izi pano poona mmene mchitidwewu wakulira ndi momwe ngozi zokhudza magetsi zikuchitikira. Nkhaniyi tidaiyamba kalekale koma pano taona kuti zanyanya ndiye palibe kuchitira mwina moti pano tayamba kale kuthothola, adatero weachiwiri kwa mneneri wa bungweli. Mneneri wa bungwe loyendetsa zisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC), Sangwani Mwafulirwa, wati ndi mlandu kupachika mbendera za chipani mmalo osaloledwa ngakhale kuti malamulo a MEC sanena chilango chomwe wopezeka akutero angalandire. Bungwe la Escom lidaletsa zipani kupachika mbendera zawo pazipangizo zake maka mapolo a magetsi ndipo lidati lidzathothola mbendera ndi zipangizo zina za kampeni zomwe zidapachikidwa kale. Bungweli lati kupatula kuti mchitidwewu ndi woopsa, zipangizo zawo zimawonongeka ndipo izi zimasokoneza ntchito zawo. Escom sidzakhudzidwa ndi ngozi iliyonse yomwe ingaoneke pomwe anthu akupachika mbendera pamapolo a magetsi, komanso idzaimba mlandu yemwe adzapezeke akupachika mbenderazi pamapolo ake. Ndipo pomaliza Escom ithothola mbendera zonse zomwe zidapachikidwa kale, chatero chikalata cha Escom. Koma ngakhale bungwe la Escom lanena kuti layamba kale kuchotsa mbendera ndi zipangizo zina za kampeni mmapolo a magetsi , mbenderazi zidajali petupetu mmizinda, mmatauni ndi mmaboma pamene kwatsala mwezi umodzi ndendende kuti chisankho chapatatu chichitike pa 20 May. ",11 " Ulangizi wabala mwana ku Mulanje Njala yomwe yakhudza madera ambiri ikuvutanso mboma la Mulanje komwe anthu akuyembekezereka kutuwa chifukwa cha mvula yanjomba yomwe adalandira nyengo ya mvula yapitayi. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Ngakhale njalayi yapereka mantha kwa ambiri, anthu a ku Mulanje West kwa T/A Juma, galu wakudayu wayamba kulambalala chifukwa cha ulimi wamthirira omwe wabonga kumeneko. Mlimi kupatutsa madzi mmunda wa chimanga Monga akufotokozera Esther Makweya wa mmudzi mwa Mlapa, langizo la alangizi awo ndilo labala zotsatira zabwino kumeneko. Alangiziwo akuti adawauza kuti akumbe zitsime ndi kuyamba ulimi wa mthirira zomwe zabereka mwana. Pano kuderali chimanga chili mbwee pamene ena akubzala, ena akukolola ndipo enanso atangwanika pamsika kukagulitsa chachiwisi. Aggrey Kamanga ndiye wachiwiri kwa wokonza za mapulogalamu ku nthambi ya zamalimidwe ya Blantyre Agriculture Development Division (Bladd). Iye adati nkhawa apachika kuti anthuwa angatuwe ndi njala chifukwa chomvera malangizo abwino. Tidawalangiza kuti ayambepo ulimi wa mthirira pokumba zitsime komanso pafupi ndi iwo pali mtsinje womwe suphwerapo. Pano aliyense ali kalikiliki ndi ulimi pamene ena tawalangiza kuti ayambiretu kupanga manyowa, adatero Kamanga. ",15 " Achitira zadama mu basi Anthu ena okhala mumzinda wa Mzuzu akhala akuchitira za dama mmabasi omwe adaimikidwa kumsika wa Zigwagwa pafupifupi miyezi inayi yapitayi. Mabasiwa, salinso mmanja mwa kampani ya Axa chifukwa banki ya FDH idawagulitsa kwa mkulu wina wa bizinesi yemwe adawaimika ku Zigwagwako poyembekezera kuwagulitsa ndi kuwaphwasula ena mwa iwo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Imodzi mwa basi amachitiramo zadamayo Komatu anthu ena apezerapo mwayi wochitiramo za chiwerewere maka yomwe idali ndi magalasi osaonekera mkati, tintedi. Msangulutso udatsinidwa khutu kuti izi zakhala zikuchitika madzulo komanso usiku ndipo kuti anthuwa amalipira kangachepe kuti apeze mwayi wodzithandiza mbasimo. Komatu si anthu a zadama okhawa omwe amapumira mmabasiwo, ngakhalenso ena osowa kogona, adatenga mabasiwo ngati nyumba zogona alendo. Pomwe Msangulutso udakazungulira pamalopo udapeza mlonda Chimwemwe Kachali yemwe adavomereza kuti wakhala akupezerera anthu akuchita chiwerewere mu imodzi mwa mabasiwo makamaka usiku. Anthu amatengerapo mwayi chifukwa ndi yosaonekera mkati ndiye zomwe amachitazo sizimaoneka kunja. Chifukwa choti chitseko chake sichitsekeka, anthu ankangolowamo, adatero Kachali. Iye adakanitsitsa zoti adalandirapo ndalama kuchokera kwa anthuwa. Mwina popeza miyezi yapitayo tidalipo awiri ndi mnzanga, ndiye kuti mwina ndi yemwe amalandira ndalama; koma ine sindidalandireko kanthu chifukwa ambiri mwa anthu omwe amachitira zadama mmenemo adali anthu woti timawadziwa ndithu, adatero Kachali. Iye adaonjezera kuti zikuoneka kuti ngakhale komwe mabasiwo adali asadagulidwe ndi bwana wake mchitidwewu umachitika chifukwa adabwera ali ndi makondomu ogwiritsidwa ntchito mwa zina. Apa adatinso masiku ena amapezanso makondomu ogwiritsidwa kale ntchito omwe anthuwo amawataya akamaliza zadamazo. Idafika nthawi yoti anthu amakuwa akamadutsa pano kuti mmabasimu mutuluka mwana ndipo ena amati aphwasulidwe kapena kugulitsidwa mwachangu, adalongosola Kachali. Iye adati zitafikapo abwana ake adayesa kuitseka ndi mawaya kuti anthu asamalowe koma sizidathandize chifukwa anthuwo adadula mawayawo. Nthawi zina ndikati ndikayendere basi pakati pausiku ndimapeza mwagona anyamata achilendo. Zikatero ndimawathamangitsa. Ambiri mwa iwo amakhala oti athamangitsidwa mnkhalango ndipo alibe kolowera, adatero Kachali. Pocheza ndi tsamba lino, mwini ma basiwo George Biyeni adati adagula mabasi asanu omwe adali a kampani ya Axa kuchokera kubanki ya FDH ndipo adalemba alonda ake awiri oyanganira mabasiwo koma mmodzi adasiya ntchito. Biyeni adati mphekesera yoti mmabasiwo makamaka ya tintediyo mumachitika za dama idamupeza ndipo adangoganiza zoyitseka ndi mawaya kuti anthuwo asamalowemo. Ndimati ndikalowa mbasimo, mumaoneka kuti anthu amachitamo zawo ndithu, koma ndikafunsa sindimayankhidwa bwinobwino, adatero Biyeni. Iye adati basi yomwe izi zimachitika kwambiriyo waiphwasula tsopano ndipo yomwe yatsala pamalopo ndi yoti omwe adawagulitsawo aikhonza kukonzekera kupita nayo ku Blantyre. Biyeni adaonjezera kuti nzovuta anthu a zadamawa kugwiritsa ntchito basi inayo chifukwa mwini wake adaikamo anthu ake angapo omwe akugona momwemo poilondera kwinaku akuikhonza. Ndipo polankhulapo mneneri wa polisi mchigawo cha ku mpoto Peter Kalaya adati ofesi yake sidalandirepo dandaulo pa nkhaniyi. Tikadauzidwa tikadafufuza ndipo ochita zadamawo akadaimbidwa mlandu wa idle and disorderlykuchita zadama malo osayenera, Kalaya adatero. ",15 "HRDC Yati Ichititsa Ziwonetsero Zatsopano Zokakamiza Ansah Kutula Pansi Udindo Bungwe lomenyera ufulu wa anthu la Human Rights Defenders Coalition (HRDC) lati lichititsanso ziwonetsero zokakamiza wapampando wa bungwe loyendetsa chisankho la Malawi Electoral Commission (MEC), Justice Dr. Jane Ansah komanso makomishonala onse kuti atule pansi maudindo awo. Trapence ndi Tembo (kumanja) Izi zanenedwa pa msonkhano wa atolankhani omwe bungweli linachititsa lolemba mu mzinda wa Lilongwe ndipo ati zionetserozi azikonza kuti zidzachitike pa 28 mwezi uno. Akulu-akulu a bungweli ati ndi odabwa kuti mpaka lero Dr Ansah sakutulabe udindo wawo ngakhale adanenetsa kuti adzatero ngati bwalo la milandu la Apilo litapezadi kuti sadayendetse bwino chisankho cha mtsogoleri wa dziko cha chaka chatha. Masiku apitawa akhala akunena kuti amadikira khoti ligamule ndipo khoti lagamula kuti sanayendetse bwino zisankho ndipo tikudabwa kuti mpaka pano sakusiya udindowu ndiye ife tikufuna tingowachotsapo tokha ndikuika munthu oti ayendetse bwino chisankho, anatero Tembo. Iwo ati ngakhale kuli nthenda ya COVID-19 ziwonetserozi zichitikabe ndipo akhala akutsata ndondomeko zomwe a unduna wa zaumoyo akhazikitsa. ",11 " CMST iyambanso kugawa mankhwala Nkhokwe ya mankhwala ya Central Medical Stores Trust (CMST) yatsiriza kukambirana ndi mabungwe omwe amathandiza dziko lino pa nkhani ya zaumoyo kuti udindo wosunga ndi kugawa mankhwala ubwerere mmanja mwake. Mkulu woyendetsa ntchito zaumoyo mdziko muno, Dr Charles Mwansambo, komanso mkulu wa CMST, Feston Kaupa, atsimikiza za nkhaniyi. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Ngoma: Ana ndi amayi amavutika Akuluakulu awiriwa ati izi zikutanthauza kuti mabungwe ndi maiko othandiza dziko lino pa zaumoyo akhutira ndi kusintha kwa ndondomeko zoyendetsera ntchito za ku nkhokweko makamaka pa chitetezo cha mankhwalawo. Apa ndiye kuti mabungwe ali ndi chikhulupiliro mu nkhokwe yathu ya mankhwala chifukwa adayamba kupereka okha mankhwala mzipatala kusolola mankhwala kutavuta mzaka za mu 2002, watero Mwansambo. Kaupa wati, mwa zina, mabungwe adatuluka mu ndondomeko yakale yodzera ku nkhokwe pogawa mankhwala pofuna kuti zinthu zina zisinthidwe ku nkhokweko ndipo zonse zatheka tsopano. Tidasintha zambiri monga chitetezo cha mankhwala mu nkhokwe, komanso pakagawidwe kake. Nkhokwe zathu nzamakono, nzovomerezeka kusungamo mankhwala, komanso tili ndi galimoto zapamwamba zokhala ndi zipangizo zoilondola kuti mankhwala asabedwe, watero Kaupa. Koma kadaulo wina pa zaumoyo Dorothy Ngoma wati ngakhale nkhaniyi ikumveka yokoma, akuluakulu aku nkhokweyo akuyenera kuganizira mozama amayi ndi ana pa ntchito yawo. Apa zikutanthauza kuti mphamvu zikubwera mmanja mwawo ndiye sitikufuna kuti posachedwapa tiyambenso kumva nkhani zogonthetsa mkhutu kuti mankhwala ena sakupezeka kapena ndiwoonongeka ayi. Zimenezi zimazunzitsa amayi ndi ana, watero Ngoma. Kadauloyu wati pomwe mabungwe ankaganiza zotuluka mndondomekoyi adaona kuti amayi ndi ana ndiwo amavutika. Choncho akhoza kukhala akuyesa ngati utsogoleri wa ku nkhokweyo wasinthadi. Chomwe chimavuta nchoti amakhalapo ena ofunadi kusintha zinthu, koma mkati momwemo mukhalanso ena atambwali ndiye tiyeni tiona kuti aziyendetsa motani, koma langizo langa ndiloti tichepetse mtima wodzikonda, watero Ngoma. Mwansambo wati mabungwe atakhumudwa ndi kubedwa kwa mankhwala, adanyanyala nkuyamba kupereka okha mankhwala mzipatala moti kuchoka 2002, kudali magulu oposa 12 osunga ndi kugawa mankhwala okha. Chomwe chimachitika nchoti padali ena osunga ndikugawa mankhwala okhudzana ndi matenda a edzi, ena amapanga za mankhwala achifuwa chachikulu, ena zauchembere ndi zina zosiyanasiyana, koma tsopano zonsezi zibwera pamodzi pansi pa nkhokwe yathu, watero Mwansambo. Iye wati izi zithandiza kuchepetsa ndalama zonyamulira mankhwala kupita mzipatala za boma chifukwa ofesi ya zaumoyo ikayitanitsa mankhwala, onse azinyamulidwa pakamodzi mmalo moti ena apititse pa wokha, enanso pa wokha. ",6 " Moyo pachiswe: Ambiri akuzemba mankhwala otalikitsa moyo Amati phukusi la moyo umadzisungira wekha, koma kumene zikuloweraku, zikuonetsa kuti Amalawi ambiri omwe ali pamndandanda wolandira mankhwala otalikitsa moyo (ma ARV) akukwirira phukusi lawo pachulu cha aganga pozemba kulandira ndi kumwa mankhwalawa. Malingana ndi zomwe Tamvani yapeza kuchokera kumgwirizano wa mabungwe olimbana ndi kufala kwa kachilombo ka HIV komwe kamayambitsa matenda a Edzi, anthu 20 mwa anthu 100 alionse oyenera kulandira mankhwalawa akuchita ukamberembere. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mankhwala otalikitsa moyo ngati awa safuna kudukiza munthu akayamba kumwa Wapampando wa mgwirizanowu, Maziko Matemba, wati ukamberemberewu ndi chiphe kaamba koti anthu otere sachedwa kugwidwa ndi chipwirikiti cha matenda chifukwa chitetezo cha mthupi mwawo chimatsika msanga. Matemba adati kupatula kutsika kwa chitetezo cha mthupi, anthu omwe amati kuyamba kumwa mankhwalawa nkudukiza thupi lawo limapima kotero kuti silimvanso mankhwala alionse omwe angalandire akamva. Tili ndi nkhawa yaikulu kwambiri chifukwa anthu otere ndiwo amabwezeretsa chitukuko cha dziko mmbuyo. Boma likuyesetsa kugula mankhwala kuti anthu ake azikhala nthawi yaitali ali ndi thanzi, koma iwo nkumathawanso, komwe kuli kusayamika, adatero Matemba. Iye adati abambo ambiri komanso omwe amakhala mmatauni ndiwo akuchulukira kuzemba mankhwalawa kaamba ka manyazi, kuiwala kuti ali ndi udindo pamabanja awo ndi dziko lomwe. Mafigala a bungwe la Malawi Network of Aids Organisations (Manaso) amasonyeza kuti mdziko muno muli anthu pafupifupi 850 000 omwe akuyenera kumalandira mankhwala otalikitsa moyo koma mwa anthuwa, mmadera akumidzi ndimo anthu ambiri amatsatira ndondomeko. Mkulu wa Manaso, Abigail Dzimadzi, adati gulu lina lomwe likuchulutsa ukamberembere ndi achinyamata omwe safuna kuonekera kuti ali ndi kachilombo poopa kuti angadzasowe mabanja mtsogolo. Chiopsezo chachikulu chili poti munthu yemwe sakulandira mankhwala ndiye ali nkuthekera kwakukulu kofalitsa kachilombo ndiye ngati achinyamata akuzemba, zikutanthauza kuti tikulimbana ndi nkhondo yomwe tikumenyananso tokhatokha, adatero Dzimadzi. Nduna ya zaumoyo, Dr Peter Kumpalume, akuti nkhaniyi ndi yomvetsa chisoni kaamba kakuti boma limafunitsitsa vutoli litatheratu mdziko muno poti ena mwa anthu omwe dziko limataya chifukwa cha vutoli ndi ofunika mipando yautsogoleri. Anthu ena auza Tamvani kuti nthawi zina anthu amazemba kukalandira mankhwala kaamba ka momwe amalandiridwira kuchipatala, koma unduna wa zaumoyo ndi bungwe la Manaso ati chifukwa ichi nchozizira polingalira za moyo wa munthu. Mpofunika kuunika nkhani ya chinsinsi cha odwala chifukwa ena safuna kuonekera koma ali ndi mtima wofuna kumalandira thandizo. China ndi malankhulidwe a ogwira ntchito kuchipatala omwe amagwetsa anthu ulesi, adatero Lucy Banda, wapampando wa gulu lophunzitsa ndi kuyendera anthu omwe ali ndi kachilombo ka HIV ku Senga Bay, komwe akuti abambo ambiri amazemba kulandira mankhwalawa nkumatangwanika ndi usodzi. Woyanganira nkhani za umoyo muunduna wa zaumoyo, Dr Charles Mwansambo, wati ichi nchimodzi mwa zifukwa zomwe boma, kudzera muundunawu, lidakhazikitsa pologalamu yoti kuchipatala kuzikhala malo apadera oti anthu azikalandirirako uphungu pankhani za Edzi ndi mankhwala otalikitsa moyo. Panopa mzipatala zambiri muli malo apadera omwe anthu amakalandirirako uphungu, kuyezetsa magazi ndi kulandira mankhwala otalikitsa moyo. Ndiye nkhani ya chisinsiyo idakonzedwa, adatero Mwansambo. Iye adatinso boma lidakhazikitsa pologalamu ya ma 90 atatu (90 90 90) kufuna kuti anthu athe kuzindikira kufunika kwa kutsatira ndondomeko ya mankhwala a ARV. Ndondomekoyi imatanthauza kuti anthu 90 alionse pa anthu 100 akudziwa momwe alili mthupi mwawo; mwa anthu 90, 90 a iwo akulandira mankhwala otalikitsa moyo moyenerera; ndipo anthu ena 90 atetezedwa kukutenga kachilomboka. Potsindika kufunika kolimbana ndi matendawa, naye sipikala wa Nyumba ya Malamulo, Richard Msowoya, adapempha aphungu a nyumbayi kuti kupatula kudalira bajeti ya boma, azikhala ndi mapologalamu opezera zipangizo zomenyera nkhondoyi. Pempholi adaliperekanso kwa akuluakulu a mabungwe pamisonkhano yomwe nyumbayi idachititsa mwezi wa August wa aphungu ndi amabungwe pankhani yolimbana ndi matendawa mchigawo cha maiko a kummwera kwa Africa, yomwe imadziwika kuti Sadc-PF. ",6 "Papa Wapempha Akhristu Amenye Nkhondo Yolimbana ndi COVID-19 Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wapempha mayiko omwe ali pa nkhondo ya pachweniweni kuti aleke kuchita izi mmalo mwake atanganidwe ndi nkhondo yolimbana ndi mliri wa Coronavirus. Papa kupemphelera anthu okhudzidwa ndi Coronavirus Iye walankhula izi ku likulu la mpingowu ku Vatican pomwe wati akugwirizana kwathunthu ndi pempho la mlembi wa mkulu wa bungwe la United Nations, Antonio Gutterez lopempha mayiko ndi magulu osiyanasiyana kuti ayambe asiya kuchita nkhondo, pofuna kuyamba nkhondo yolimbana ndi nthenda ya COVID-19, yomwe yavutitsa dziko la pansi. Pamenepa Papa wati nkhondo yolimbana ndi mliri wa Coronavirus ingayende bwino ngati pali ubale wabwino pakati pa anthu a mitundu yosiyana. Mwazina Papa Francisco wapempha anthu omwe akumachitirana zamtopola kuti kuchita izi sikungabweretse kusintha kulikonse pokhapokha atakhala pansi ndi kukambirana, zonse zingatheretu. ",6 " Mafumu akusunga zitupa za ena Pamene gawo lachitatu la kalembera wa chisankho cha pa 21 May 2019 akuyembekezeka kutha mawa mboma la Lilongwe, anthu ena adandaula kuti akulephera kulembetsa chifukwa mafumu akusunga ziphaso zawo. Mmadera ena omwe Tamvani adazunguliramo, ena adandaula kuti mafumu adawalanda ziphaso za unzika ndipo akupereka ndalama kuti awabwezere zitupazo popita kokalembetsa pomwe mmadera ena akuti anthu akulephera kukalembetsa chifukwa cha miyambo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Zopingazi zaululika pomwe zipsinjo zimene zidalipo mgawo loyamba ndi lachiwiri makamaka zokhudza kuvutavuta kwa zipangizo ndi kamemedwe ka anthu zikuoneka kuti zakonzedwa. Anthu pamalo olembetsera a Malembo kwa T/A Khongoni mbomali Lolemba adati akulephera kukalembetsa chifukwa zitupa zawo za unzika zili ndi mafumu omwe akufuna ndalama kuti awabwenzere zitupazo. Mndondomeko ya kalembera wa ulendo uno, bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) likugwiritsa ntchito chitupa cha unzika chokha ngati umboni woti munthu alembetse mkaundula ndipo popanda chitupachi, munthu sakuloledwa kulembetsa. Mmodzi mwa anthuwo, Moses Phiri, wa mmudzi mwa Salamba adati mafumu adatenga zitupazo ati pofuna kulongosola za kaundula wa sabuside. Mafumu ndi a zamalimidwe adatenga kuti apangire kaundula wa makuponi a sabuside koma akuti pali chikonzero choti mudzi ulionse upereke ndalama yopangira kaundulayo ndiye tikupereka ndalama kwa amfumu kuti akulembe kenako nkukubwezera chitupa chako, adatero Phiri ataombola chitupa chake ndi K500. Woyanganira malo olembetserawo Ezala Nacford adatsimikiza kuti zitupa za anthu ambiri zili ndi mafumu zomwe zikupangitsa kuti anthuwo azilephera kulembetsa. Tabweza mafumu angapo atabwera ndi zitupa zambirimbiri kuti adzalembetsere anthu. Malamulo salola izo. Titafufuza, tapeza kuti eni zitupazo akulephera kukazitenga chifukwa sakupereka ndalama, adatero Nacford. Woyanganira za zisankho ku bungwe la MEC Sammy Alfandika Lachiwiri adati kusunga chitupa cha wina ndi mlandu ndipo adachenjeza kuti aliyense yemwe ali ndi chitupa cha mnzake akuyenera kubweza. Aliyense ayenera kusunga yekha chitupa chake chifukwa chingafunike nthawi iliyonse osati ya kalembera yokha, adatero Alfandika. T/A Khongoni adadabwa atamva nkhaniyi ndipo adati aitanitsa mafumu onse a mdera lake kuti awafunse nkhaniyo ndipo akatsimikiza aona momwe athanirane ndi mafumu omwe akukhudzidwa ndi mchitidwewu. Mmalo ena monga Sonkhwe, Tsachiti, Kasemba ndi Kamphata kwa T/A Kalumbu, ogwira ntchito adadandaula kuti anthu sakufika mwaunyinji kukalembetsa chifukwa cha miyambo. Pa Sonkhwe, anthu 1 698 ndiwo akuyembekezeka kulembetsa koma pofika Lolemba lapitalo, anthu 866 ndiwo adali atalembetsa ndipo woyanganira pamalowo, Lemson Solomon, adati zinthu sizikuyenda chifukwa cha miyambo. Kukuoneka kuti ino ndi nyengo ya ziliza ndi maukwati koamnso chiyambireni kalembera, kwachitika maliro akuluakulu angapo zomwe zachititsa kuti anthu azitanganidwa mmidzi, adatero Solomon. Pamalo olembetsera a Tsachiti, anthu 2 120 akuyenera kulembetsa koma pofika lolemba, anthu 1 115 ndiwo adali atalembetsa ndipo woyanganira malowo David Chikumba adati mmasiku 6 oyambirira, kudagwa maliro anayi mmidzi yozungulira. Kupatula maliro, woyanganira malo olembetsera a Kasemba, Laika Palikena, adati mderalo mudali miyambo ya ufumu iwiri ndi ziliza zomwe zidatangwanitsa anthu. Poyamba kudali mwambo okwenza amfumu a Chimbalame ndipo pano mwambo olonga umfumu wa a Ndunga uli mkati. Kupatula apo kudali maliro atatu komanso ziliza ndiye zinthu sizikuyenda ayi, adatero Palikena. Mkulu wa bungwe la MEC Jane Ansah adati zopinga zokhudza miyambo nzokulira bungwelo koma nzongofunika kukambirana bwino ndi mafumu kuti awone momwe angakonzere zinthu kuti kalembera asasokonekere. Miyambo ngati imeneyi komanso maliro ndi zinthu zomwe zimakhalako nthawi zonse chaka chonse kaya kuli kalembera kapena ayi ndiye nzotikulira koma tiyesetsa kukambirana ndi mafumu, adatero Ansah. Ngakhale zili chonchi, bungwe la National Initiative for Civic Education (Nice) Trust lati akukhulupilira kuti akwanitsa chiwerengero cha anthu omwe akuyembekezera kulemba mgawoli. ",8 "Sakundikwatira Agogo, Ndithandizeni. Ndili paubwenzi ndi mwamuna yemwe adakwatirapo koma banja lake lidatha ndi mkaziyo ndipo kuli mwana mmodzi. Inenso ndili ndi mwana mmodzi. Titatha chaka tili pachibwenzi adandiuza kuti andikwatira koma mpaka lero padutsa zaka 4 palibe chimene chkuchitika. Foninso adasiya kundiimbira, komanso pan chikondi chachepa. Nditani? BH Zikomo BH, Mwamunayo si wachilungamo ndipo akungokunamiza, za banja alibe nazo ntchito. Ngati ukuti pano zaka 4 zatha chikuuzireni kuti akufuna akukwatire ndipo olo foni sakukuimbiranso, ufuniranji umboni wina woti alibe nawe chikondi? Usataye naye nthawi ameneyo, udzangodikirapo madzi a mphutsi apa. Palibe chako. Akadakhala kuti ali ndi chidwi nawe pano atakaonekera kwa makolo ako ndipo pano bwenzi tikukamba kuti muli pabanja. Ndidalirebe? Agogo, Ndifunse nawo. Ine kwathu ndi ku Rumphi ndipo ndakhala ndili pachibwenzi ndi mnyamata wa ku Mzimba kwa zaka ziwiri tsopano. Sitinagonanepo ndipo tinagwirizana zotengana koma mpaka pano chaka chikuthanso. Ndikamufunsa akuti akonzeke kaye. Kodi ndipange bwanji? Ndidalirebe? Zikomo pondilembera kuchoka ku Rumphiko. Funso lovuta kuyankha mwana wangakodi udalirebe? Inde ndikuti eee, usataye mtima poti kuona maso a nkhono nkudekha. Ngati mnyamatayo akuti akonzeke kaye, mwina akunena chilungamo. Ndi anyamata ochepa amene amatha kukhala pachibwenzi ndi mtsikana kwa zaka ziwiri osagonana naye. Sindidziwa, paja amati mtima wa mnzako ndi tsidya lina, koma mmene ndikuonera fatsa, zoona zake zioneka zokha. Iwe ukuthamangira banja chifukwa chiyani? Mwamunayo ngwanzeru nchifukwa chake akuti akonzekere kaye za ukwati, osangoti lero ndi lero basi tikwatirane uku alibe chilichonse. Ndikudziwa bwino lomwe kuti ku Mzimba ndi ku Rumphi miyambo yokhudza ukwati imafanana, mwamuna akafuna kukwatira amayenera kupereka malobolo, si choncho? Ndiye mwina akusakasaka kaye kuti akamatuma thenga kwa asewere akhale ndi kenakake mmanja, osati kungopita chimanjamanja. Chachikulu nchoti simudagonanepo ndipo ngati ukuona kuti akukunamiza ukhoza kumusiya nkupeza wina amene watsimikiza za ukwati. Nthawi zambiri atsikana ena zikawavuta, tiyese kuti mwatsoka achimwitsidwa ndi wina pamene ali pachibwenzi ndi winanso, amakakamira wachikondiyo kuti akwatirane msangamsanga ncholinga choti azikati pathupi mpamwamunayo! Ndikhulupirira sizili chonchi ndi iwe. Ofuna Mabanja Ndine mayi wa mwana mmodzi ndipo ndikufuna mwamuna wodziwa mavuto, wachikondi, woopa Mulungu koma wopanda banja. 0884 437 604 Ndili ndi zaka 23 ndipo ndifuna mwamuna woti ndimange naye banja. Akhale woti akufunadi banja osati zoyesana ayi. Wofuna aimbe pa: 0992 673 004 Ndine mayi wa ana awiri ndipo ndifuna mwamuna womanga naye banja. Akhale wachilungamo komanso woopa Mulungu.0992 728 276 ",15 " Mnyamata asiya sukulu chifukwa cha mantha A makhumbira atakhala msirikali, koma popanda moyo ntchitoyi singatheke. Lero Christopher Robert, mnyamata wachialubino, wasankha kaye moyo posiya sukulu yomwe ati ikadamuphetsa. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Zochitika pa 6 May 2016, pamene mnyamata wina wosamudziwa adafika pasukulu pawo kudzamutenga ndi zomwe zachititsa kuti thupi la Christopher lichite tsembwe ndi mantha kuti moyo wake ukhoza kukhala pachiswe ndipo walembera aphunzitsi ake kuti wasiya sukulu. Mphunzitsi wamkulu pasukulu ya Mwatonga, kwa T/A Kasumbu mboma la Dedza, wauza Msangulutso kuti patsikulo mnyamata wina adafika pasukulupo nkunena kuti watumidwa kudzamutenga Christopher, wa zaka 18, yemwe ali kalasi 6, chifukwa akumufuna kupolisi ya Dedza. Amati watumidwa, koma nditaimba kupolisi, adandiuza kuti ndimumange, ndipo ndidaterodi, adatero mphunzitsiyu, Felix Mussa. Akuti moyo wake uli pachiopsezo: Christopher Adatsagana ndi mayi ake a Christopher ndi achitetezo cha mmudzi ulendo kupolisi komwe ati adakadzidzimuka akuuzidwa kuti amupepese mnyamatayo chifukwa chomunjata popanda chifukwa. Ine limodzi ndi mayi a Christopher komanso achitetezo tidamupepesa ndipo adamumasula pomwepo, adatero Mussa. Mnyamatayo, yemwe ndi wabisinesi, adauza Msangulutso kuti: Adati ndikatenge amfumu, makolo a mwana ndi mwanayo kuti abwere kupolisi adzafunse zina ndi zina chifukwa amati kunyumba kwawo kudapitako anthu amene ankafuna akamube, adatero iye. Mathedwe a nkhaniyi adatutumutsa Christopher ndipo mantha adayanga thupi lake nchifukwa adaganiza zolembera mphunzitsi wamkuluyu kuti sukulu waisiya. Zikomo Ahedi. Muli kudziwitsidwa kuti ndayamba ndasiya sukulu chifukwa cha nkhani yomwe inachitika Lachisanu. Ndiye ndaona kuti sindingathe kuphunzira chifukwa ndingathe kumakhala ndi maganizo komanso poweruka ndimakhala ndekha ndiye njira ndiyaitali chosadziwika chondichitikra munjiramu pamene ndili ndekha paja poyamba ndinafotokoza kale ndiye panopa ndili pankhawa ngati pangakhale kusamvetsa pazomwe ndanenazi munene tsiku kuti ndibwere kuti tidzakhambirane. Zimene ndinafuna kudziwitsani ndi zomwezi. Ndine Christopher, ikutero kalaya yomwe adalemba Christopher. Mtolankhani wa Msangulutso atamupeza kunyumbako, kudali kovuta kuti alankhulane naye. Adadzitsekera mnyumba, ngakhale ahedi a Mussa, amfumu komanso achibale ena adamuuza kuti asaope, iye adakanitsitsa poganiza kuti mtolankhaniyu wabwera kudzamuba. Padatha mphindi 30, ndipo Christopher adatuluka, mayi ake atakambira naye. Nkhope yakugwa, iye adakhala patali ndi mtolankhaniyu. Ndili wachisoni kuti ndasiya sukulu. Ndimakhumbira nditakhala msirikali, koma basi sindidzakhalanso msirikali chifukwa sukulu ndasiya, adayamba kufotokoza Christopher, amene adakhala nambala 4 mkalasi teremu yatha. Iye adati sakuganizanso atabwerera kusukulu chifukwa chilungamo sichidayende pankhani yake. Ndi bwino andiphere pakhomo pano kusiyana kuti akandiphere kusukulu. Izi zidandipatsa mantha ndipo ndidaganiza zolemba kalatayo kuti ndasiya sukulu. Nakonso kukwaya sindikupita ndipo ndikungodzitsekera mnyumbamu, adatero Christopher, amene bambo ake banja lidatha ndi mayi ake. Wachiwiri kwa mneneri wa polisi ya Dedza, Cassim Manda, adavomera kuti mnyamata amene adapita kusukulu ya Christopher adamutulutsa chifukwa adamangidwa mlandu wosaudziwa. Tikufuna tifufuze kaye ndiye tamutulutsa. Kungoti pali zomwe zidachitika ndiye tikufufuza, adatero Manda, ponena kuti sangayankhe mafunso ambiri pafoni koma pamaso. Ngakhale mutu weniweni wa nkhaniyi sukudziwika bwinobwino, Christopher akuti sabwereranso kusukulu, komwe amayenda makilomita 7 kuchoka kunyumba kwawo. Padakalipano mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika wapempha amipingo kuti athandizepo kuti mchitidwe wopha ndi kusowetsa achialubino otheretu. ",3 " Andale agundika misonkhano, osapewa Covid-19 Msabatayi, anthu ena 5 adapezeka ndi kachirombo ka coronavirus mdziko muno, kuchititsa kuti chiwerengero cha anthuwo chifike pa 63. Chiopsezo cha nthendayi chikukulirakulira. Koma zikuoneka kuti andale sakusamala za izi, pomwe akuchititsa misonkhano mosalabadira kuti nkhani ya gulu ndi chinyezi chofalitsa matendawa. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Atangopereka zikalata zawo kwa wapampando wa bungwe la zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) Jane Ansah, Lazarus Chakwera yemwe akutsatizana ndi Saulos Chilima mumgwirizano wa zipani za Malawi Congress Party (MCP) ndi UTM Party adazungulira mumzinda wa Blantyre komwe chikhamu chimasonkhana, osapereka mpata wokhala mita imodzi. Ndipo atapereka zikalata zawo, mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika yemwe akuimira zipani za Democratic Progressive Party (DPP) ndi womutsatira wake Atupele Muluzi wa United Democratic Front (UDF) nawo adazungulira mumzindawo mosalabadira za khamu lofikako. Ndipo Lamulungu, Chakwera ndi Chilima adachititsa msonkhano kubwalo la Mzuzu Upper Stadium, pomwe Muluzi adali pamisonkhano yoimaima kuchoka ku chigawo cha kumwera mpaka pakati. Monsemo, kudalibe kutsata ndondomeko yotalikana. Koma akadaulo ena pa zaumoyo ndi ndale ati zipanizi zikuika miyoyo ya anthu pachiswe chifukwa matenda a Covid-19 ndi oopsa. Kadaulo pa zaumoyo Maziko Matemba wati ndale zili apo, atsogoleri a zipani akuyenera kutsatidwa. Kampeni imayenera kutha pa 30 June koma chifukwa choti tsiku la chisankho silinaikidwe, onse okhudzidwa ayenera kudziwa kuti kapmeni iyenera kutha masiku kuchokera tsiku la chisankho, adatero iye. Koma kadaulo wa malamulo Sunduzwayo Madise adati MEC ili ndi udindo wosankha tsiku la chisankho, monga lichitira posankha tsiku la chisankho chapadera. Nyumba ya Malamulo idakhazikitsa tsiku pofuna kutsata malamulo a chisankho kuti psakhale chisokonezo chifukwa nkhani ya chisankho cha patatu chiyenera kutsatidwa. Koma MEC ili ndi mphamvu yokhazikitsa masiku atsopano, monga imachitira pakakhala chisankho chapadera cha aphungu kapena makhansala, adatero Madise. Wapampando wa komiti ya zamalamulo ku Nyumba ya Malamulo Kezzie Msukwa adati adzidzimuka ndi nkhaniyi. Nzodabwitsa kuti MEC ikufuna kuti chisankho chidzakhaleko pa 23 June, adatero Msukwa. Ndipo msabatayi, akachenjede a zamalamulo apempha Mutharika kuti alemekeze chisankhocho pochotsa makomishona a MEC omwe bwalo lamilandu lidawapeza kuti sadayendetse bwino chisankho cha pa 21 May 2019. Mmodzi mwa akachenjedewa, Garton Kamchedzera wa ku Chancellor College adati anthu ali tcheru kuyembekeza tsiku lomwe Mutharika adzachotse makomishonala nkusankha ena. Nchifukwa chiyani sakufuna kutula pansi maudindo? Ndikuona kuti zikanakhala bwino akanatula maudindo awo pa okha. Kupanda kutero, anthu okhanza kupanga chiganizo pazosatira za chisankho chomwe chikubwerachi ndipo kupitirira kukhalabe maofesi sikovomerezeka mmalamulo. Ndipo Mutharika akuyenera kuchitapo kanthu pogwiritsa ntchito section 75 ya malamulo. Gawo 75 ndime 4 imaperka mphamvu kwa mtsogoleri wa dzko kudzera kubungwe la Public Appointment Committee (PAC) ya ku Nyumba ya Malamulo ikapeza kuti komishoniyo ilibe kuthekera koyendetsa masankho. Mipando ya makomishonayo itha pa 5 June pomwe iwo akwaniritse ndime yawo. ",11 "Akagwira Ukayidi Kaamba Kodyetsa Mwana Chimbudzi Bwalo loyamba la milandu mboma la Kasungu lalamula a Hickson Banda a zaka 26 zakubadwa kuti akakhale ku ndende ndi kukagwira ntchito ya kalavulagaga kwa zaka zitatu kamba kowapeza olakwa pa mlandu odyetsa chimbuzi mwana wake omupeza. Wachiwiri kwa wofalitsa nkhani za apolisi mbomalo Sergeant Miracle Mkozi waudza Radio Maria Malawi kuti a Banda adapalamula mulanduwu pa 22 April ndipo mayi a mwanayu atakatula nkhaniyi ku polisi ndi pomwe anamangidwa tsiku lomwelo. Popereka chigamulo chake First Grade Magistrate Damiano Banda adati zomwe adachita a Banda podyetsa mwana chimbudzi ndi zosemphana ndi gawo 240 la malamulo a dziko lino, choncho akuyenera kuti akagwira ukayidi kwa zaka zitatu kuti anthu ena atengerepo phunziro. Panali pa22 April pomwe a Hickson Banda a zaka 26 anasiyiridwa mwana ndi akazi awo omwe anapita kuchigayo ndipo pobwera anapeza kuti mwanayo wadyesedwa bibi ndipo akaziwo anabwera kuzanena ku polisi, anater Mkozi. ",7 "2019 MSCE Results Out By Thokozani Chapola ele.jpg"" alt="""" width=""452"" height=""320"" />Has released the results-Susuwele Banda The Malawi National Examinations Board (MANEB) has released the 2019 MSCE examination results. According to the annouced results, a total of 98,332 candidates had registered for the examination but 92,867 sat for the examination. The results have been announced by Minister of Education, William Susuwele Banda through a statement. Out of the 92,867 candidates who sat for the examination, 46,771 have passed. This represents 50.36 % pass rate. Out of the 41,708 female candidates who sat for this examination 17,887 have passed. This represents 42.89% pass rate. Out of the 51,159 male candidates who sat for this examination 28,884 have passed. This represents 56.46% pass rate. Out of 573 Special Needs candidates who sat for this examination 302 have passed. This represents 52.71% pass rate. The results of 6 candidates have been withheld pending investigations for contravening MANEB regulations, reads the staterment. The MANEB has also released a list of ten best performing schools in this years MSCE examinations are as follows: Loyola Jesuit Secondary School of Kasungu Marist Secondary School of Dedza Mlare Secondary School of Lilongwe East Lilongwe Islamic (Pvt) Secondary School of Lilongwe West Pius X11 Seminary of Chiradzulu Ludzi Girls Secondary School of Mchinji Zomba Catholic Secondary School of Zomba Urban St Marys Secondary School of Zomba Urban Marymount Catholic Girls Secondary School of Mzuzu City Johns ( Pvt ) Secondary School of Lilongwe City According to the same MANEB, The ten best candidates in this years MSCE examinations are as follows: Ranking Candidate Name Sex Centre Name Aggregate points 1 Arthur Promise Chibondo M Zomba Catholic Secondary School 6 2 Lusako Mwaisango M Chaminade Secondary School 7 3 Misheck A. Masamba M Blantyre Secondary School 7 4 Ruth Paul Bizeck F St. Marys Secondary School 7 5 Yamikani Watson M Zomba Catholic Secondary School 7 6 Bland Benson Mtchona M Maranatha (Pvt) Secondary School 7 7 Harris Ecrem Majamanda M Robert Blake Secondary School 7 8 Gowokani Mkandawire M Chaminade Secondary School 8 9 Wilned Kanyimbo M Marist (Pvt) Secondary School 8 10 Leonard Kadzamira M Marist (Pvt) Secondary School 8 The minister has however congratulated MANEB for releasing free, fair and credible examination results. ",3 " Gwamba wochokera kubanja loimba Mdziko muno muli oimba osiyanasiyana. koma kukamba za oimba nyimbo zauzimu, Gwamba ndi mmodzi mwa oimba amene akusintha miyoyo ya anthu pa Malawi pano. STEVEN PEMBAMOYO adacheza naye motere: Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Gwamba: Ndi nyimbo zokoma kwambiri Gwamba, ndimasule kuti ndikudziwe bwinobwino mmachezawa. Dzina langa lonse ndi Duncan Gwamba Zgambo omaliza mbanja la ana anayi ndipo kwathu ndi mboma la Rumphi ku mpoto kwa dziko la Malawi. Anthu ambiri amangoti Gwamba, tawauze kuti kodi Gwambayo ndi wotani ndipo amakonda chiyani. Zikomo kwambiri, Gwamba ndi dzina lomwe ndimatchukadi nalo ngati oyimba koma munthune ndimapanga zambiri monga mabizinesi ndi zina. Kuimbaku ndi chimodzi mwa zochita zomwe ndimapanga pamphepete pa mabizinesi. Kodi iweyo zoimbazi udayamba bwanji? Funso labwino ndipo anthu ambiri amandifunsa zimenezi moti ndikayankha iweyo ndiye kuti ndayankha anthu ambiri nthawi imodzi. Munthune ndimachokera ku banja la zoimbaimba. Malume anga, Bright Nkhata, adali munthu waluso kwambiri pa zoimba moti ambiri amamudziwa bwino. Kupatula apo, malume anga ena, Bernard Kwilimbe, nawonso ndiwokonda zoimba kwambiri moti oimba ena mMalawi muno adaphunzira kwa anthu awiri amenewa. Mwachidule, zoyimbazi ndi za mmagazi osati kuchita kuphunzira kapena kukakamiza ayi. Watulutsa chimbale posachedwapa, kodi udachitulutsa liti ndipo chimatchedwanji? Chimbale chimenechi chikutchedwa Jesus is my Boss kutanthauza kuti Ambuye Yesu ndi bwana wanga. Ndi nyimbo ya uzimu yokoma kwambiri ndipo ili ndi tanthauzo ndi chiphunzitso chapamwamba kwa okhulupilira. Chimbale chimenechi chidakhazikitsidwa pa 24 December 2016 ku Bingu International Convention Centre (BICC) ija ena amati 5 Star Hotel. Chimbalechi chili ndi nyimbo zingati ndipo zina mwa izo ndi ziti? Chimbalechi chili ndi nyimbo 11 ndipo papita luso ndikudzipereka kuti chituluke ndi kumveka momwe chimamvekeramu. Kudatengera kudzipereka kwa anthu angapo monga oimba, ojambula ndi azipangizo omwe. Muli nyimbo monga Anabwera Yesu yomwe ndimayikonda kwambiri komanso ndiyo yoyambirira. Mulinso nyimbo yotchedwa Bwana yomwe adathandizira Lulu ndipo nayonso ndi nyimbo yokoma kwambiri. Mwachidule, nyimbo zomwe zili mchimbalechi nzokoma zokhazokha. ",9 "Radio Maria Itsekera Nyengo ya Mariatona Wolemba: Richard Makombe A Director a Radio Maria Malawi Bambo Joseph Kimu ati wayilesiyi ikukwanitsa kufalitsa uthenga wabwino wa yesu khristu ngakhale ili ndi ngongole zoposa 50 million kwacha. Bambo Joseph Kimu amayankhula izi pa mwambo wa nsembe ya ukaristia otsekera nyengo ya Mariatona omwe unachitikira ku Mtendere Parish mu dayosizi ya Dedza. Bambo Kimu ati ndiokondwa kuti anthu ambiri amamvera wayilesiyi kuphatikizapo anthu omwe si a mpingo wa katolika zomwe anati ndi chisonyezo kuti zikulimbikitsa anthu kukonda kupemphera. Anali mlendo wolemekezeka pa mwambowo- a Bonga ndi akazi awo Pali anthu ena ambiri omwe amathandiza wayilesiyi omwe ndi a mipingo ina ndipo izi zapangitsa kuti Radio Maria ikhale ikufalitsa uthenga wabwino wa yesu khristu kuyambira pomwe inatsegulidwa zaka 20 zapitazoanatero Bambo Kimu. Bambo Kimu anapitiliza kupemph anthu onse akufuna kwabwino komanso akhristu kuti apitilize kuthandiza komanso kuyikonda wayilesiyi kuti izikwaniritsa cholinga chake chofalitsa uthenga wabwino kwa anthu ambiri. Ndikupempheni kuti mupitilize kupemphelera Radio Maria komanso muzikonda kugwiritsa ntchito wayilesiyi mu zochitika zanu kuti uthenga wa mulungu upilire kufalikira ponseponseanapitiliza motero Bambo Kimu. Bambo Kimu anati Ndikudziwa kuti muli ndi mavuto a zachuma pano pa Parish komanso mmanyumba mwanu koma munaona kuti nkofunika kuti muthandize Radio Maria ndithokoze kuti mwaonetsa chikondi chomwe muli nacho ku wayilesiyi Mmawu awo Monsignor John Chithonje anati akuthokoza a Director a wayilesiyi kamba kosankha kudzachitira mwambo otsekera Mariatona ku dayosizi ya Dedza zomwe ati zikusonyeza ubale wabwino omwe ulipo pakati pa dayosiyi yi ndi Radio Maria Malawi. Dayosizi ino ndiyokonzeka kuthandiza Radio Maria nthawi ina iliyonse ndipo timayesetsa kuthandiza kuti ntchito zake zipitilire kupita patsogolo anateroMonsignor Chithonje. Monsignor Chithonje anathokoza kwambiri akhristu a Parishi yi kamba kotenga gawo pothandiza wayilesiyi zomwe anati zaonetsa ubale omwe ulipo ndi wayilesiyi komanso kuti amayikonda Radio Maria. Ntchito yomwe Radio Maria ikugwira yathandiziranso kuti ubale wathu ndi akhristu a mdziko la Mozambique ukhale opambana komanso wamphamvundipo zaonetseratu kuti akhristuwa amakonda kumvera wayilesiyianatero Monsignor Chithonje Nyengo ya Mariatona inatsegulidwa ku Sacred Heart Zomba Cathedral ku Zomba dayosizi pa 4 May ndipo yatsekedwa pa 27 July 2019 ku Mtendere Parish mu dayosizi ya Dedza. Pa mwambowu ndalama zokwana 1 million six hundred and fifty 9 hundred forty kwacha ndi zomwe zinapezeka ndipo mlendo olemekezeka pa mwambowu anali a Mike Bonga omwe anapereka cheke cha ndalama zokwana 5 hundred thousad kwacha. ",13 " Youth Week ibwereredi Achinyamata, mafumu Mtsogoleri wa achinyamata pa ndale wa bungwe la Young Politicians Union Clement Mukuwa wati ndi wosangalala ndi ganizo la boma lofuna kukhazikitsanso sabata ya achinyamata (Youth Week) chifukwa likugwirizana ndi zomwe achinyata adaika pamndandanda wa zolinga zawo. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Tili ndi mndandanda wa zomwe tikufuna achinyamata atamachita ndipo chimodzi mwa izo ndi kugwira ntchito modzipereka ndiye tikakumbuka zomwe Youth Week inkachita, zikugwirizana ndi mfundo imeneyi, adatero Mukuwa. Kudikira kuti boma likonze: Munthu kuoloka movutikira paulalo woonongeka Phungu wa kumpoto cha kummawa kwa boma la Mchinji, Alex Chitete, ndiye adayambitsa nkhaniyi mNyumba ya Malamulo pomwe aphungu amaunika momwe chuma cha dziko chayendera pamiyezi isanu ndi umodzo (6). Phunguyu adapempha boma kuti likhazikitsenso sabata ya achinyamata monga zidalili mnthawi ya ulamuliro wa malemu Dr. Hastings Kamuzu Banda pomwe achinyamata mdziko muno adali ndi sabata yogwira ntchito zachitukuko mmadera awo pofuna kuwaphunzitsa za ubwino wogwira ntchito modzipereka potukula dziko lawo. Iye adati panthawi ya ulamuliro wa chipani chimodzi achinyamata ankatenga gawo lalikulu pachitukuko kusiyana ndi masiku ano pomwe kuli ntchito zogwira ndi chiyembekezo cholandira dipo yomwe akugwira ndi anthu akukuluakulu. Poyankhapo, nduna ya zantchito Henry Mussa adati ganizoli si loipa koma silokakamiza ndipo mmapulani a boma muli kale ndondomeko zomwe akuti achinyamata azipatsidwa mpata kutenga nawo mbali pantchito zina. Iye adati mundondomekoyi, ntchito zina zomwe zizigwiridwa ndi zachitukuko monga momwe zinkakhalira mnyengo ya Youth Week kalelo. Tidayankha kale pankhani imeneyo kuti si zokakamiza koma ndondomeko ilipo kale moti pompanopompano ziyambika, adatero Mussa. Mukuwa adati ngati mtsogoleri wa achinyamata pandale akhoza kukhala wokondwa anthu atadziwitsidwa ubwino wa Youth Week ndi zolinga zake kuti mtima wogwira ntchito wodzithandiza posayembekezera malipiro ubwerere mwa Amalawi. Katswiri pa mbiri ya dziko lino, Desmond Dudwa Phiri (DD Phiri), ndi mafumu angapo akuluakulu ati ganizo lokhazikitsanso sabata ya achinyamatali ndi lofunika kwambiri pachitukuko cha dziko la Malawi. DD Phiri adati Youth Week ndi nyengo yomwe achinyamata ankatengapo mbali pachitukuko chosiyanasiyana ngati nzika za dziko mwaulere ndipo izi zinkathandiza kutula midzi ndi madera omwe ankakhala. Nthawi imeneyi achinyamata ankakhala otangwanika kwambiri pantchito zachitukuko monga kukonza misewu, milatho, zipatala, sukulu ndi zina mmadera mwawo mwaulere ndipo zinthu zinkayenda, adatero mkhalakaleyu. Iye adati ntchito ngati zomwezi, pano zimalira bajeti yaikulu kuti anthu agwire, mapeto ake ndalama zikasowa, zitukukozi zimayamba zaima kwa nthawi yaitali, zinthu nkumapitirira kuonongeka. Youth Week inkakhalako chaka chilichonse nyengo ngati ino ya Pasaka ndipo tinkadziwiratu kuti misewu yonse yoonongeka, milatho, zipatala, sukulu ndi nyumba za aphunzitsi zomwe zikuonongeka zikonzedwa. Pano ntchito ngati zimenezi zimalinda ndalama za mbajeti kuti anthu kapena makontirakitala azigwire. Ngati ndalamazo palibe, ndiye kuti zinthuzo zizingopitirira kuonongeka mpaka ndalama zidzapezeke, adatero DD Phiri. Mkuluyu adati Youth Week idatha mdziko muno mutabwera ulamuliro wa zipani zambiri poganiza kuti idali nkhanza kwa anthu (thangata) ndipo mmalo mwake boma lidasenza lokha udindo wogwira ntchito zachitukuko. Iye adati koma anthu sankaona Youth Week ngati thangata ndipo ankagwira ntchito modzipereka ndi umodzi mpaka pomwe adauzidwa kuti ndi thangata. Mkulu wodziwa za mbiri yakaleyu adati maiko ambiri omwe ndi otukuka pano adayamba ndi eni ake kudzithandiza ndipo boma linkangobwera pambuyo kudzawonjezera pomwe paperewera. Mfumu yaikulu (T/A) Maseya wa ku Chikwawa akugwirizananso ndi ganizoli ponena kuti achinyamata amaphunzira ntchito zosiyanasiyana panyengoyi chifukwa amasakanikirana ndipo omwe adali ndi luso amagawira anzawo pogwira ntchitozo. Iye adati kudzera mnjira imeneyi, achinyamata amakula ndi mtima wokonda ntchito ndiposo zimawathandiza kukhwima mmaganizo kuti paokha akhoza kupanga chinthu chooneka popanda kuyanganiridwa. Zidali zokoma kwambiri moti zitati zayambiranso zikhoza kukhala bwino kungoti nzofunika kuti poyambitsapo aunike bwinobwino kuti ntchitozo angazigawe motani potengera zaka kuti zisakolane ndi nkhani yogwiritsa ana ntchito yoposa msinkhu wawo, adatero Maseya. Inkosi Chindi ya ku Mzimba idasangalalanso ndi ganizoli ponena kuti nyumba zambiri zophunziriramo, zokhalamo aphunzitsi, milatho ndi misewu zomwe pano zili ngati bwinja zikhoza kukonzedwa mosavuta. Chitukuko cha kudera ndi udindo wa anthu okhala kudera limenelo ndiye anthu atafotokozeredwa bwinobwino phindu lomwe angapeze kuchoka muntchito zachitukuko cha Youth Week, sindikukhulupirira kuti angawiringule, adatero Chindi. Iye adati munyengoyi, achinyamata amagwira ntchito zosiyanasiyana monga kulambula misewu, kukonza milatho, nyumba za aphunzitsi ndi zitukuko zina uku akutayitsa nthawi ndi macheza. Naye T/A Mkanda ya mboma la Mchinji idati ana ambiri masiku ano amalephera kupita kusukulu nyengo ya mvula kaamba kolephera kuoloka mitsinje chifukwa chodikirira kuti boma likonze milatho. ",10 " Tigwirane manja pothana ndi chisaka cha Nthochi Mkulu woona za mbewu za mgulu la zipatso ku dipatimenti ya za kafukufukuku mu unduna wa zamalimidwe Felix Chipojola akuti nkhondo yolimbana ndi matenda a chisaka cha nthochi mdziko muno siingaphule kanthu pokhapoka anthu atagwirana manja. Iye adafotokoza kuti njira yokhayo yothana ndi chisaka ndikuchotsa nthochi zonse zakale ndikubzala zina. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kukakamira nthochi zakale kukuchititsa kuti chisaka chizipitirira Chipojola adati mzomvetsa chisoni kuti alimi ena sakufuna kudzula nthochi zawo zakale zomwe zikuchititsa kuti matendawa asathe msanga mdziko muno. Tidakagwirana manja ndikuonetsetsa kuti nthochi zonse zakale zachotsedwa, matendawa akadatha ndipo mdziko muno bwenzi mukupezeka ntchochi zochuluka, iye adatero. Malingana ndi mkuluyu, ngakhale alimi omwe adachotsa nthochi zakale ndikubzala zopanda matenda ali pachiopsezo cha matendawa chifukwa amzawo sakufuna kudzula nthochi zawo zakale zomwe zikhoza kuchititsa za tsopanozo kuti ziyambenso kugwidwa ndi matendawa. Chipojola adati matenda a chisaka cha ntchochi amafala ndi nsabwe zomwe zimatha kuulukira mminda ina. Ena akumaputsitsika akaona nthochi zawo zikuoneka za thanzi koma akuyenera kudziwa kuti matendawa amabisala ndipo tsiku lina amadzavumbuluka, iye adatero. Woona za ulimi wa mbewu za mtunduwu kwa Bvumbwe Harold Katondo adati adayendera mmaboma momwe mumalimidwa kwambiri nthochi mdziko muno ndicholinga chofuna kupeza zomwe zikuchititsa kuti alimi azikakamirabe mbewu zakale. Pocheza nawo alimiwa amafotokoza kuti mbewu zawo zakale nzokoma kwambiri komanso amatha kuzigwiritsa ntchito kuphikira zinthu zosiyanasiyana. Chodabwitsa nchoti ngakhale amayankhula zoterezi, sadayetserepo kulima kapena kudya nthochi zatsopanozi, iye adatero. Katondo adati izi zachititsa kuti ayambe kutolera mbewu zakalezi mmadera osiyanasiyana a mdziko muno ndikuzikonza kuti zikhale zopanda matenda. Iye adati akazikonza ndikuzichulukitsa adzazibwezera kwa alimi kuti azidzabzala. Mkulu wa za ulimi mboma la Thyolo Jackson Mkombezi adati alangizi mbomali adayesetsa kuwafotokozera alimi za njirayi koma ntchito ya kalavula gaga yomwe imakhalapo pochotsa ntchochi ndiyomwe ikuchititsa kuti mbewu zakale zizipezekabe. Ntchitoyi ikadakhala yosavuta ikadayenda mwachangu ndipo nthochi zambiri zikadachotsedwa ndikubzalidwa zina zopanda matenda, iye adatero. Mkuluyu adati alimi omwe adabzala mbewu zopanda matenda mu 2015 pano akutsimba lokoma ndipo ambiri akupeza zokolola zamnanu. Mulanje ndi limodzi mwa maboma omwe ulimiwu umachitika kwambiri moti mkulu wa za ulimi mbomalo Evelyn Chima akuti kuchepa kwa mbewu ndi ena mwa mavuto omwe amachititsa kuti azikakamirabe mbewu zakale. Poyambirira tidalandira mbewu yochepa moti alimi omwe adavomereza kubzala mbewu zopanda matenda sadalandire onse. Chaka chino talandira mbewu yochuluka komanso alimi ena tawaphunzitsa kuti azitha kuchulukitsa ndikumagaira anzawo. izi zithandizira kuti anthu ochuluka apeze mbewu, iye adatero. Chima adati alangizi a mbomali akuyesetsa kugwira ntchitoyi ndi atsogoleri a mipingo, mabungwe komanso zipani ndi cholinga chofuna kupititsa patsogolo ulimiwu. ",4 "Sitima Ya Papa Francisko Ikupulumutsa Miyoyo Sitima ya pa madzi yotchedwa Papa Francisco ikupereka thandizo la chipatala ku madera a mtsinje wa Amazon mdziko la Brazil. Malinga ndi malipoti a Vatican Radio sitimayi ikupereka chithandizo cha zipangizo za mchipatala kumidzi ya pafupi ndi mtsinje wa Amazon kwa anthu omwe akuvutika chifukwa cha mliri wa Coronavirus. Sitimayi akuti yapulumutsa miyoyo komanso kubweretsa chiyembekezo pakati a anthu a ku deralo. Pamene mliri wa Coronavirus ukupitilira kuvutitsa maiko ambiri anthu a ku dera la mtsinje wa Amazon mdziko la Brazil ndi oyamika kaamba ka sitima ina ya pa madzi yotchedwa Papa Francisco yomwe ikuthandiza anthu ku deralo ndi zipangizo za mchipatala pa nthawi iyi ya mliri wa Coronavirus. Sitimayi ili pa ntchito yolimbana ndi mliri wa Coronavirus pothandiza omwe akudwala komanso kuteteza awo omwe sanagwide ndi nthendayi. Malinga ndi Joel Sousa bulazala wa chipani cha Francisco Woyera wa ku Assisi, sitimayi akuti yabweretsa chiyembekezo komanso yapulumutsa miyoyo ya anthu ambiri ku deralo. Sitimayi yakhala ikuthandiza anthu ku deralo kuyambira mwezi wa July mchaka cha 2019 ndi chithandizo cha chipatala koma kuti panopa ogwira ntchito mu sitimayi ali pa ntchito yolimbana ndi mliri wa Coronavirus. A bulazala komanso ansembe a chipani cha Francisco Woyera wa ku Assisi ndiwo eni ake a sitimayi ndipo iwo akuti analimbikitsidwa pa ntchito yopereka chithandizo cha chipatala kwa anthu mderalo ndi Papa Francisco pomwe anali ku Brazil pa chaka cha achinyamata (World Youth Day) mchaka cha 2013. Sitima yotchedwa Papa Francisco yi ili ndi anthu 23 odziwa ntchito za chipatala, zipinda momwe anthu amalandira thandizo, chipinda chopangira ma opareshoni, chipinda chopimira anthu mmene aliri mthupi mwao pongotchula zochepa chabe. Dziko la Brazil ndi limodzi mwa maiko omwe akhudzidwa kwambiri ndi mliri wa Coronavirus pokhala pa nambala 2 pa mndandanda wa maiko omwe chiwerengero cha anthu omwe agwidwa ndi nthenda ya Covid 19 ndi chokwera kwambiri. Anthu pafupi 1.9 million agwidwa ndi nthenda ya Covid 19 mdziko la Brazil kutsatira dziko la United States of America lomwe lili pa nambala 1 pa chiwerengero cha anthu omwe agwidwa ndi nthenda ya Covid 19. Malinga ndi malipoti a pa 14 July 2020 a sukulu ya ukachenjede ya John Hopkins anthu 72,833 amwalira ndi nthenda ya Covid 19 mdzikolo. Ndipo ndi pa tsiku lomweli la 14 July 2020 pomwe likulu la Mpingo wa Katolika pa dziko lonse linalengeza kuti Papa Francisco watumiza thandizo ku dzikolo la zipangizo zothandiza anthu omwe akuvutika kupuma bwino kuti athe kupuma mosavutika (ventilators). ",14 "Papa Wadzudzula Mchitidwe wa Tsankho Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco walimbikitsa anthu pa dziko lonse kuti akuyenera kumachita zinthu mosakondera kamba koti izi ndi zomwe zimasangalatsa Mulungu. Papa Francisko Iye wanena izi pakutha pa mwambo wa mapemphero a lero mmawa ku likulu la mpingo-wu ku Vatican. Iye wati pofuna kupereka thandizo la mtundu wina uliwonse anthu akuyenera kuti azipewa kuchita tsankho kamba koti izi ndi zosayenera pa maso pa Mulungu. Iye wati Mulungu akamapereka thandizo ndi chisamaliro chake samayanganira khalidwe la munthu kaamba koti chikondi chake ndi chopanda malire. ",14 "Dziko la Ghana Latsekula Malo Opemphelera President wa dziko la Ghana Nana Akufo-Adodo watsekula malo opempherera omwe anatsekedwa pofuna kupewa kupatsirana kwa kachilombo koyambitsa nthenda ya COVID-19 mdzikolo. Walengeza za nkhaniyi- Akufo-Addo Malipoti a wailesi ya BBC ati malowa ndi monga matchalitchi komanso mizikiti ndipo anthu osaposa 100 ndi omwe akuloredwa kumasonkhana mu nthawi yosapitilira ola limodzi. Anthu omwe akusonkhana mmalo opemphelerawa apemphedwa kupitiliza kutsatira njira zopewera kupatsirana matendawa monga kukhala motalikirana komanso kuvala chotchinga kukamwa ndi mphuno (Mask) pomwe akupemphera. Mwazina presidenti-yu wati kuwonjezera apo ophunzira a mchaka chomaliza ayambanso kupitiriza maphunziro awo ndipo mzipata zolowera mdzikolo zikhalabe zotseka. Ganizoli ladza pomwe chiwerengero cha anthu opezeka ndi nthendayi chaima pa 8,060 omwe ndi kuphatikizapo 36 omwe amwalira ndi nthendayi. ",13 " Khama lipindula paulimiPhungu Nthawi zambiri chomwe chimasowa paulimi ndimasomphenya. Alimi ambiri amangolingalira zoti ndikakolola chaka chino ndidzalimanso chaka cha mawa mmalo moti azilingalira kuti chaka chino ndalima ndipo chaka chamawa ndidzakhale pena. Phungu wa kunyumba yamalamulo wa ku mpoto kwa boma la Mangochi Benedicto Nsomba ndichitsanzo chabwino pankhaniyi. Iye adayamba ngati mlimi ochulukitsa mbeu nkusuntha kufika pogulitsa mbeu ndipo pano ali ndi kampani yakeyake yopanga mbeu. STEVEN PEMBAMOYO adacheza naye motere: Nsomba: Mbewu zanga nzovomerezeka ndi boma Ndikudziweni olemekezeka. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ine ndine Benedicto Chambo ndipo, monga mwanena kale, ndine phungu wa ku Nyumba ya Malamulo woimira anthu a kumpoto kwa boma la Mangochi. Kunyumba ya Malamuloko ndilinso mukomiti ya zaulimi komanso pandekha ndimalima kwambiri. Inu mulinso ndi kampani yopanga mbewu, kodi mbiri yanu ndi yotani? Za inetu anthu ambiri sakhulupirira ayi. Ndidayamba zaulimi ngati mlimi wochulukitsa mbewu pansi pa gulu la Association of Smallholder Seed Multipliers Action Group mchaka cha 2005. Nditachitapo ulimiwu ndidasuntha nkuyamba kugulitsa mbewu nditatsegula Chambo Agro- Dealers ku Mangochi komweko. Ndagulitsa mbewu mpaka kufika pomwe ndimatsegula kampani yanga yopanga mbewu ya Pindulani Seed Company. Chiyambi chake nchotani? Mchaka cha 2010 ndidaona kuperewera kwa mbewu za gulu la nyemba pamsika ndiye ndidaganiza zoyamba kupanga mbeuzi. Ndapangapo mbewu za mgulu la nyemba kwa zaka ziwiri mpaka kufikira mchaka cha 2013 pomwe ndidaonjezera nkuyamba kupanganso mbewu ya chimanga kufikira pano. Muli ndi msika wa mbewu zanu? Kwambiri ndipo mbewu zanga ndi zimodzi mwa mbewu zomwe alimi ambiri akukonda chifukwa zimamera ndi kubereka mwapamwamba kwambiri. Mwinanso ndikuuzeni pano kuti boma lidavomereza mbewu zanga moti pano zili mupologalamu ya zipangizo zotsika mtengo ya sabuside. Apa ndikutanthauza kuti mbewu ina yomwe alimi alime kuchokera musabuside ya mgulu la nyemba komanso chimanga ndi yopangidwa ndi kampani yanga ya Pindulani. Mumapanga mbewu yochuluka bwanji pachaka? Poyamba penipeni ndidayamba ndi matani 10 okha ndipo ndimanka ndikukwera pangonopangono mpaka pano ndidakula ndithu. Chaka chino ndapanga matani 340 a mbewu zosiyanasiyana za mgulu la nyemba ndinso matani 150 a chimanga chamakono chopirira ku ngamba chomwe boma ndi akatswiri akulimbikitsa. Ndili wokondwa kuti mbewu zonsezi zidatengedwa mupologalamu ya sabuside. Inu mbewu zanu mumazitenga kuti? Si njere iliyonse yomwe ili mbewu. Nzoona, si njere iliyonse ungabzale nkumati ndi mbewu. Ine ndili ndi alimi anga ochokera kudera langa omwe ndimagwira nawo ntchito. Ndimawapatsa mbewu kuti achulukitse ndipo ndimawagula pamtengo wabwino ngati njira imodzi yowatukulira. Alimi ambiri panopa kudera kwanga adatukuka moti amangamanga nyumba zamakono za malata kumeneko kuchokera mu ntchito imeneyi. Tinene kuti mudaima pambewu zamitundu iwiriyi basi? Ayi, ndiye kuti mutu wasiya kuganiza. Lingalirani komwe ndikuchokera kudzafika pano ndiye ndiimire pano? Pakalipano tikuchita kafukufuku wa mbewu za mtedza ndi nyemba zoyenera mthirira zomwe zotsatira zake zikatuluka tikhala tikulimbikitsa alimi kuti azichita ulimi wamthirira wa mbewuzi. Kupatula apo, tikuchitanso katupe wa mbewu zamakono za chinangwa ndi mbatata zamthirira moti ntchito imeneyi yakhala pangono kutha kuti tiyambe kugulitsa mbewu yake. Eni makampani opanga ndi kugulitsa mbewu amadandaula za akamberembere omwe amakopera mbewu zawo nkumaononga mbiri yawo, kaya inu mudakumanapo nazo zotere? Zimenezo nzoona, akamberembere alipodi koma chimachititsa kwambiri ndi ogwira ntchito kumakampaniko omwe ali osakhulupirika chifukwa ndiwo amatenga mapaketi nkumakagulitsa kwa akamberemberewo kuti aziikamo mbewu yachinyengo. Komabe pobwerera kufunso lanu, ife zimenezi sitidakumanepo nazo chifukwa tidapanga njira yoti mapepala a umboni aja amati seal oika mkati mwa paketi, timapanga tokha ndiye olo atapeza mapaketi athu, seal ikhoza kuwasowa. Alimi ambiri amakakamira pamodzimodzi zaka nkumapita, inu mungawauzenji? Nkhani yaikulu ndi kukhala ndi masomphenya basi. Kumaona patali kuti kodi ineyo lero ndili pano nanga mawa ndidzakhale pati? Mlimi akakhala ndi maganizo otere, zinthu zimayenda chifukwa amayesetsa kuti maloto ake aja akwaniritsidwe, asafere mmalere. China, pamafunika kulimba mtima pochita zinthu chifukwa ukakhala ndi mantha ndiye sizingakuyendere mpangono pomwe. Kupatula kuyendetsa kampani ya mbewu, pali china chokhudza ulimi chomwe mumapanga? Ndili ndi sikimu zingapo ku Mangochi komwe ndimachitirako ulimi wamthirira wa mbewu zosiyanasiyana. Ndidalemba alimi oposa 1 500 nkuwagawira malo musikimumo kuti azilima. Akakolola, ndimawagula mbewuzo pamtengo wabwino komanso zina zimakhala zawo zakudya pakhomo. Mwezi wa October alimi adakolola nyemba zambiri ndipo ndidawagula zonse pamtengo wa K600 pakilogalamu moti pano ambiri ali ndi ndalama, savutika nyengo yachisangalaloyi. ",4 " Mayi amwalira kokafuna golide Mayi wa zaka 36 wamwalira ku Salima pamene dothi la mumtapo wa golide yemwe amafunafuna litamugwera iye ndi mwamuna wake. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mneneri wa apolisi ku Salima Gift Chitowe watsimikiza za nkhaniyi pouza Msangulutso Lolemba lapitali kuti nkhaniyi idachitika pa 8 January chaka chino pamene mayi womwalirayu, Elinati Mkaundu, pamodzi ndi mwamuna wake adanyamuka kumudzi kwawo kupita kumudzi wa Sadzu komwe ankafuna kukayesera mwayi wawo kokafuna miyala yamtengo wapatali yotchedwa galanayiti. Chitowe adati atafika kumalo komwe kunali mtapoko mayiyo ndi mwamuna wake adafikira kulowa mdzenje la mtapolo ndi kuyamba kufunafuna miyala ija koma mwatsoka dothi lomwe lidali mudzenjemo lidawagwera ndipo mayiyu adamwalira pomwepo pamene mwamuna wake adavulala thupi lonse ponyukanyuka. ",6 "Chiwerengero Chamatenda Opatsirana Chakwera Kwambiri Mmaiko a mu Africa-WHO By Glory Kondowe .radiomaria.mw/wp-content/uploads/2019/07/who-300x150.jpg"" alt="""" width=""452"" height=""226"" /> Bungwe lowona za umoyo pa dziko lonse la World Health Organisation (WHO) lati chiwerengero cha anthu omwe akugwidwa ndi matenda a chikuku ndinso matenda ena opatsirana chakwera kwambiri chaka chino mmaiko ambiri a mu Africa. Malinga ndi malipoti a news24, bungwe la WHO lati chiwerengero cha anthu opezeka ndi matendawa, chakwera ndi 700% mchaka chino chokha cha 2019. Bungweri lati izi zikuchitika chifukwa maikowa sakupereka katemera wa matendawa mokwanira kwa anthu awo kuti chiwerengero chamatendawa chitsike. ",6 " Adatuma nthenga kudzandifunsira Kudali ku Dedza, mwezi wa October mchaka cha 2017 pomwe Lucy Mvula adalandira uthenga kuchokera kwa mzake wa Geoffrey Kishombe. Uthengowo umati Kishombe akulephera kugona kotero akumufuna chibwenzi. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Koma Lucy sadaugwiritse ntchito uthengawo chifukwa choti wobweretsa nthengayo adali ankakonda kuledzera ndipo pomwe ankapereka uthengawo patsikulo nkuti atalawa pangono. Koma nthengayo adabweranso tsiku lina maso ali gwaa kudzatsindika za khumbo la Kishombe. Ndipo adandipatsa nambala ya phone ya nzawoyo ndipo ine ndidapereka yanga, adatero Lucy. Lero ndi thupi limodzi: Banja la a Kishombe Apatu awiriwo adakhala masiku ndithu osayankhulana mpaka pomwe tsiku lina Kishombe adamuimbira Lucy ndipo ichi chidasanduka chizolowezi kufikira tsiku lomwe adagwirizana zoti akumane. Tsiku lokumana litafika, Kishombe, pamodzi ndi anzake ena awiri adapita kunyumba kwa Lucy kukacheza, zomwe zidachititsa kuti macheza awo agwire moto. Mosakhalitsa, Kishombe adafunsira ndipo naye Lucy sadazengereze koma kulola. Ndidatengeka kwambiri chifukwa cha momwe ankandizondera. Ankakonda kuimba foni kungofuna kudziwa za moyo wanga, adatero Lucy. Awiriwo adakhala pa ubwenzi kwa zaka ziwiri kufikira pa November 19 2019 pomwe adalowa mbanja ndipo madyerero adachitikira pa Greek Orthodox Garden, mu mzinda wa Blantyre. Awiriwo ati mavuto awo amathana nawo poyangana kwa Mulungu. Lucy amagwira ntchito yaunamwino ndi uzamba pomwe Kishombe amagwira ntchito ku bungwe la Malawi Bureau of Standards (MBS). Pakadali pano awiriwo akukhalira ku Chigumula mu mzinda womwewu wa Blantyre koma Lucy amachokera ku Euthini, mfumu Chindi mboma la Mzimba ndipo Kishombe amachokera mmudzi mwa Mwafilaso, mfumu Kyungu mboma la Karonga. ",15 " Chiyembekezo pa ntchito zakunja Ofuna ntchito ku Lilongwe ngati awa akufuna boma likonze zolakwika Pamene boma lalengeza kuti likulingalira zoyambanso kutumiza achinyamata kukagwira ntchito kumaiko ena, osowa ntchito ena ati ngakhale ndondomekoyi ndi yabwino, akukayika ndi momwe amasankhira okagwira ntchito kunjako. Mneneri wa unduna wa za ntchito, Joyce Maganga, adati ntchito yotumiza achinyamata kunja imene idayamba muulamuliro wa Joyce Banda ipitirira. Iye adatsutsa kuti chipani cha DPP chidaimika ntchitoyi, imene achinyamata 100 000 amayenera kupeza mwayi wa ntchito ku South Korea, Quatar ndi Dubai. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Chifukwa choti ntchitoyi idayamba ndi mtsogoleri wakale wa dziko lino, sizikutanthauza kuti ikuyenera kuimitsidwa kapena kutayidwa. Mtsogoleri wa dziko lino [Peter Mutharika] ali ndi ndondomeko zatsopano zopitirizira pologalamuyi, adatero Maganga. Malinga ndi nduna yakale ya achinyamata, Enoch Chihana, boma limafuna kuti achinyamata 2 000 atumizidwe kunja koma lidangokwanitsa kutumiza 800 okha, makamaka ku Dubai. Achinyamata 15 000 adayesa mwayi wawo pachilinganizo choyamba koma adapeza mwayi sadapose 1 000. Koma achinyamata ena, ati akukayika ngati osauka apindule pachilinganizochi. Alfred Limbani wa zaka 29 ndipo amakhala ku Area 36 mumzinda wa Lilongwe adati adakondwera pomwe adamva kuti boma la Joyce Banda liyambitsa ndondomekoyi. Koma mvula ya masautso ake a ulova sidakate momwe amayembekezera. Ndidakondwa nditamva kuti kukudza mwayi wa ntchito. Koma sindidamve bwinobwino kuti opitawo amawasankha bwanji. Adatenga achinyamata. Zoti chilinganizochi chipitirira ndi nkhani yabwino koma tipemphe boma latsopanoli kuti libweretse poyera ndondomeko zotengera achinyamata ena ulendo uno komanso enafe tipindule nawo, adatero Limbani. Sibongile Manda, wa zaka 26, adati boma likuyeneranso kubwera poyera malinga ndi malipoti ena oti achinyamata ena amene adapeza mwayiwo amazunzika. Boma liyenera kukayendera kaye malo antchitowo kuti lionetsetse kuti achinyamata sakukumana ndi mavuto kumeneko. Komanso litenge ambiri kuti nafenso tipeze chochita, adatero Manda. Izi zidapherezera lipoti la Amnesty International limene mmbuyomu lidasonyeza kuti maiko monga South Korea ndi Qatar amazunza ogwira ntchito awo, makamaka amene akugwira ntchito zammunsi komanso ochokera kumaiko akunja. Komatu chiyembekezochi sichili ndi achinyamata okha. Nawo akuluakulu monga Cydric Brazilo wa zaka 35, ali maso kunjira. Koma iye adati zachinyengo zimene zimachitika pandondomeko ya mmbuyomu zisakhaleko. Pologalamuyi tidaimva koma anthu timafooka nayo chifukwa choti kasankhidwe ka achinyamata okagwira ntchitoyi kamaoneka ngati kachinsinsi. Tikuona ngati adapita abale awo a akuluakulu a boma okha basi. Mnzanthu wina adapereka K15 000 nkulembedwa dzina kuti apita koma adamuyenda pansi. Pano akadali lova kwawo ku Kasiya, adatero iye. Kulipira ndalama kotere, malinga ndi Patrick Bvumbwe wa zaka 44, nkusupula amphawi amene akufuna ntchito. Mmbuyomu zimamveka kuti wofuna ntchito apereke ndalama, tsono amphawife tizipeza kuti ndalamazo? adatero iye. Malinga ndi Maganga, ntchitoyi idakumana ndi mikwingwirima ku South Korea kokha. Ngakhale boma linkati lidagwirizana ndi boma la South Korea kuti litumizako achinyamata, mmodzi mwa akuluakulu oona za kunja kwa dzikolo Moon Sung Hwan adati padalibe mgwirizano ulionse pakati pa maboma awiriwo. Vuto tinali nalo ndi lokhudza dziko la South Korea. Kumeneku kokha ndiye ntchitoyi tidaimitsa kaye. Koma kumaiko a Dubai ndi Kuwait ikupitirira, adatero mneneriyo. Mlembi wamkulu wa ungano wa mabungwe oyanganira apantchito wa Malawi Congress of Trade Union (MCTU), Elijah Kalichero, adati bungwelo lakhala likutsutsana ndi ndondomekoyi chifukwa achinyamata ambiri amakumana ndi zokhoma kumaiko achilendoko. Takhala tikulandira malipoti oti achinyamata ambiri amazunzidwa ndi kugwira ntchito zakalavulagaga kumaiko kumene amapitako. Komanso ambiri akugwira ntchito zosiyana ndi zimene adalonjezedwa. Ena akufunitsitsa atabwerera kuno kumudzi, adatero Kalichero. Tidalephera kulankhula ndi nduna ya zantchito Henry Mussa kuti timve ndondomeko zimene boma lakonza kuti mavuto amene adalipo mmbuyomu athe chifukwa samayankha foni yake. ",15 " Tidakhulupirirana tsiku loyamba Chikondi chidayambira kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College komwe Dennis Lupenga akuti atakumana ndi Sheila Chimphamba mchaka cha 2013 pomwe onse amachita maphunziro, adakhulupirirana tsiku lomwelo. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Awiriwa adamaliza maphunziro awo ndipo Sheila amagwira ntchito muofesi ya mapolojekiti komanso ndi mkonzi wa mapologalamu kuwayilesi ya Zodiak pomwe Dennis ali ndi kampani yake ya zamakina a Internet. Dennis akuti ubale wa awiriwa udayamba pa 9 April chaka chokumanacho Awiriwa tsopano ndi thupi limodzi cha 2013 iye atauza njoyelo mwachindunji kuti akufuna kumukwatira osati za chibwenzi monga momwe anthu ambiri amayambira. Ndidalibe nthawi yotaya nkumati ndili pachibwenzi chifukwa Sheila adandigwiriratu mtima ndipo ndidalibeso nthawi yoti ndimuone kaye ayi, adatero Dennis. Iwo akuti ngakhale uku kudali kusukulu, mmaganizo mwawo mudalibe za chibwenzi koma kuti akungoyembekezera tsiku lodzalowa mbanja ndipo panthawi yonseyi sadasiye makolo ndi abale awo mumdima pozindikira kuti ubale wawo sudali wachibwana. Titakambirana, tidadziwitsa abale ndi makolo kuti azidziwa chifukwa timazindikira kuti pokangopita nthawi pangono tiwafuna kuti atimangire chinkhoswe ndi kutigwira dzanja pomwe tikukalowa mbanja, adatero Dennis. Iye akuti adakhala choncho mpaka chaka cha 2014 pa 9 August pomwe adamanga chinkhoswe nkuyamba kukonzekera ukwati omwe udachitika pa 2 April ku tchalitchi cha Katolika cha Maula ndipo madyerero adali ku Peak Gardens mumzinda wa Lilongwe. Sheila ndi mkazi wanzeru, wokongola, wachilungamo, wodzisamala ndi woopa Mulungu. Adandiwonetsa chikondi chenicheni monga momwe makolo anga adandionetsera, adatero Dennis. Dennis ndi mwamuna wolimbikira, wodzichepetsa ndi wachikondi komanso wachilungamo. Amandilimbikitsa ndikakhala ndi chofooka ndipo amandiphunzitsa kuthana ndi zokhoma, adatero Sheila. ",15 "Papa Afunira Zabwino Atolankhani Akatolika Omwe Akuchita Maphunziro Wolemba: Glory Kondowe Aku-likulu la mpingo wakatolika ku Vatican afunira zabwino atolankhani a mpingowu omwe akuchita maphunziro awo mdziko la Ivory Coast. Mmodzi mwa akulu-akulu a ku ofesi ya zofalitsa nkhani ku likulu la mpingo-wu ku Vatican, Paolo Ruffin, ndi amene wapereka uthenga-wu kuyimira mtsogoleri wa mpingo-wu pa dziko lonse. Papa Franscico Mwazina uthenga womwe akulu ampingo wakatolika ku Vatican anatumizira atolankhaniwo ndi wolimbikitsa kuti akuyenera kugwira ntchito zawo mwa ukatswiri ndi kuwonetsetsa kuti akuthandiza kulimbikitsa ntchito zachilungamo ndi zina zambiri. Maphunziro omwe akonzedwa ndi bungwe la ngwilizano watolankhani achikatolika ACJ mogwirizana ndi ndinthambi yofalitsa nkhani mumpingo mudzikomo mothandizana ndi mkulu ofalitsa mawuthenga muzikomo abuye Raymond Ahowa. ",3 " Chitetezo chibwerera mchimake Mkulu wapolisi mdziko muno Lot Dzonzi wati uchifwamba omwe anthu ambiri akudandaula kuti wafika povuta tsopano utha chifukwa cha njira zina zomwe apolisiwa akonza. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Dzonzi adanena izi pomwe amatsegulira msonkhano wolimbikitsa mgwirizano wa apolisi ndi anthu popititsa patsogolo chitetezo omwe unachitikira kulikulu la polisi ku Lilongwe Lolemba. Iye adati a polisi omwe agwira bwino ntchito aziwapatsa mphoto zikuluzikulu monga kukwenzedwa pa ntchito nyengo ya Khirisimasi komanso zina za ndalama. Dzonzi adati likulu la polisi lakonzanso ndondomeko yotumiza apolisi ambiri mmatauni ndi mmadera omwe azikakhalira komweko kuti azigwira bwino ntchito yawoyo ndipo aziwayendera kuona mmene ntchitoyi ikuyendera. Titumiza a polisi ambiri mmadera onse ndipo tiziwayendera pafupipafupi kuti tiziona mmene ntchito ikuyendera. Pambali potumiza a polisi ambiri, kumapeto kwa chaka chilichonse tizikhala ndi mwambo wopereka mphoto zikuluzikulu monga kukweza apolisi omwe agwira ntchito bwino komanso kuwapatsa ena ndalama kutengera ndi mmene agwirira ntchito yawo, adatero Dzonzi. Iye adaonjeza kuti akudziwa za mavuto amene apolisi amakumana nawo mmadera momwe akukhala ndipo adatsimikizira apolisiwa kuti zinthu zisintha posachedwa chifukwa awakhazikitsira maofesi pafupipafupi. Pamsoknhanowo, apolisi ena komanso maofesi a mmaboma adalandira mphoto chifukwa chogwira bwino ntchito ndipo Dzonzi adapempha apolisi onse makamaka a pansewu kuti azikhala a ulemu ndiomvetsetsa. Timvetsetsane apa. Sikuti kugwira bwino ntchito ndikumanga anthu kokhakokha koma kuwaunikira pomwe akuoneka kuti akusochera. Komabe pochita izi, tikuyenera kuonetsetsa kuti tikuteteza anthu olakwiridwa, adatero Dzonzi. Yunus Lambat yemwe anali wapampando wa bungwe loyendetsa za mgwirizano wa apolisi ndi anthu adati pazaka ziwiri zokha, bungweli lakhazikitsa maofesi okwana 27 000 mdziko muno omwe amayanganira ntchito za chitetezo ndipo adapempha komiti yatsopano kuti ipitirize ntchitoyi. Mkulu wa bungwe loona za ufulu wa anthu la Centre for Human Rights and Rehabilitation, Undule Mwakasungula, adati apolisi achita bwino kuganiza zokhazikitsa njirazi chifukwa anthu akuzunzika ndi uchifwamba. Mwakasungula adati nkofunika kuti a polisi aganize zokhazikitsa njira zambiri zoti anthu azidziwitsira apolisi pamene akumana ndi zovuta kapena aona anthu okayikitsa. ",7 "MET Yachenjeza za Mvula Yamphamvu Nthambi yowona za nyengo ndi kusintha kwa nyengo yati mvula yamphamvu ikuyembekezeka kugwa mmadera ambiri mdziko muno kuyambira lero mpaka lachisanu pa 14 February 2020. Malinga ndi chikalata chomwe chasayinidwa ndi mkulu wa nthambiyi Jolam Nkhokwe, mvulayi yomwe ikhale yosakanikirana ndi mphepo yamphamvu, komanso ziphaliwali ikuyembekezeka kugwa mmadera a kumwera, pakati komanso madera a mbali mwa nyanja. Mvulayi akuti ikuyembekezeka kudzetsa kusefukira kwa madzi mmadera otsika komanso momwe mumachitika-chitika ngozi za mtunduwu kaamba koti padakalipano dothi lidakali lonyowa mmadera ambiri mdziko muno. Mwazina mphepo yamphamvuyi komanso ziphaliwali, zili ndi kuthekera kowononga zinthu, kuvulaza komanso kupha anthu. Pamenepa nthambiyi yapempha anthu kuti asamuke mmadera omwe ndi angozi, apewe kuwoloka mitsinje pamene yadzadza komanso kupewa kubisala pansi pa mitengo ndi nyumba zina zosalimba, pofuna kupewa ngozi zomwe zingadze kaamba ka nyengoyi. ",18 "Bungwe la TC Lachititsa Maphunziro Ozindikiritsa Adindo za Malamulo Mchitidwe ogwiritsa ntchito ana mminda ya fodya akuti ungachepe ngati adindo atatsatira moyenera malamulo omwe adakhazikitsidwa oyendetsera ulimi wa fodya mdziko muno. Mmodzi mwa akuluakulu a bungwe lowona za ulimi ndi malonda a fodya mdziko muno la Tobacco Commission (TC) a Hellings Nason ndi omwe anena izi pambuyo pa maphunziro ozindikiritsa adindo, ena mwa malamulowa. A Nason anati mchitidwewu ukukula mchigawo chapakati cha dziko lino ndipo adindo akuyenera kuchitapo kanthu kuti izi zithe. Mfundo zina zomwe zili mmmalamulo amenewa zinafunikira kuti tizifotokozere kwa iwo amene akhoza kuthandizira kuti lamulo liyambe kugwira ntchito moyenera monga mafumu amene amakhala kumidzi ndi anthu ndi amene angakwanitse kuwafotokozera anthu, anatero a Nason. Poyankhulapo komishonala owona za milandu a Samawat Chisale anadandaula kuti milandu yochepa yokha ndi yomwe imafika ku polisi ndipo anati maphunzirowa athandizira kuti anthu adziwe za malamulo. ",4 " Mwambo wopha mudzi poika mfumu Anthu ena amakhulupirira kuti akamwalira amayenera akaikidwe chatsonga kapena kuti chokhala. Izi zimachitika kwambiri pakati pa mafumu Achingoni maka a kwa Maseko. Umu ndi momwe zidakhalira ndi maliro a T/A Bvumbwe wa ku Thyolo mwezi wathawu, yemwe adaikidwa chatsonga. Anthu otere akamwalira, pamakhala mwambo wopha mudzi. Izi zimachitika pokumba nyumba yoti igone mfumuyo. BOBBY KABANGO akutsata momwe zimakhalira. Pepani wawa ndi zovutazi. Koma ndimati tichezepo pangono za miyambo ina yokhudza maikidwe a mfumu Yachingoni. Koma poyamba tidziwane. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Ndine Opesi Mangombo ndipo kwathu ndi mommuno mwa Bvumbwe. Ndinu wa mtundu wanji? Mukadzaona nsalu ya Gomani chonchi komanso mthini pamutu, musadzafunse, dziwani kuti amenewo ndi Angoni ankhondo aja amene adachoka ku Mozambique ku Domwe. Moti ine ndi Mngoni, ndili kumtundu wa Bvumbwe. Ndamva kuti inu ndiye mumatsogolera adzukulu okumba manda a mfumu Mwamva zoona koma si kuti ndi manda onse, koma kuti ndinatsogolera adzukulu amene akumba manda amene tiike thupi la mfumu yathu Bvumbwe. Timamva za mawu oti kupha mudzi pamene mukukumba manda ogona mfumu, zimatanthauzanji? Choyamba dziwani kaye kuti mfumu yathu igona chatsonga, kupha mudzi kumachitika ngati mukukumba manda a munthu amene akaikidwe chatsonga. Kwa iwo okaikidwa chogona ndiye sikukhalanso kupha mudzi. Mudzi ndi malo kapena kuti phanga lomwe mfumuyo imaikidwako. Choyamba mumakumba dzenje lotalika ndi mamita atatu ndi theka. Limakhala dzenje lozungulira, osati lamakona anayi monga zikhalira ndi ena. Mukamaliza kukumbako ndiye mumakhala pansi kupanga mudziwo. Fotokozaninso, mwati mudzi nchiyani? Mudzi ndi malo kapena kuti phanga lomwe mfumu igoneko. Pamene mwakumba ndi kumaliza manda, ndiye mumayamba kupanga phanga. Kukula kwake kufanane ndi kukula kwa bokosilo. Koma nthawi zambiri mudziwo umakula ndi mamita awiri mlitali ndi mlifupi. Ndiye mukati kupha mudzi mumatanthauza chiyani? Timatanthauza ntchito yomwe mumachita kuti muyambe kupanga phangalo lomwe kulowe mfumu yathu. Zimatheka bwanji kuti mupange phanga loti muli kale mdzenje? Timaonetsetsa kuti dzenjelo likhale lokula bwino kuti mukathe kukhala pansi ndi kumagoba mudziwo. Timapangira khasu lomweli koma timaligulula ndi kulizika ngati nkhwangwa. Mukamaliza mumatani? Tikafikira mlingo womwe tikufuna, timatenga timitengo ndi kukhoma pakhomo pa mudziwo chifukwa bokosi likalowa, timayenera titseke pakhomopa kuti dothi lisalowe. Simungapange mudzi musadayeze kukula kwa bokosi lomwe mfumu yathu igonemo. Dothi lakenso liti? Pajatu dzenjeli timalikwirira pamene taika mfumu yathu, ndiye pakhomo pa mudzi timatsekapo kuti dothi lisamupeze. Koma cholinga chopangira mudziwu nchiyani? Mfumu siyenera kuthiridwa dothi pamutu. Mudziwu umapangidwa dala kuti ipeze kobisala pamene tikuthira dothi. Ndi manda ngati awa, chiliza chake chimakhala chotani? Chimamangidwa mozunguliranso (akuloza ziliza za mafumu ena pamandapo) osati chogona monga zina zimakhalira. Malo ano ndi a mafumu okhaokha komanso akazi awo. Mwana wa mfumu sagona pano pokhapokha ngati wavekedwa ufumu. Kodi uku sikungovutika chabe? Mwatero ndi inuyo koma ife sitiona kuvutika koma kukwaniritsa chikhalidwe chathu ndi ulemu kwa mafumu athu monga Angoni. ",1 "St. Augustine Parish Yati Ipilira Kuthandiza Achinyamata Mmasewero Achinyamata ku parish ya Augustine woyera mu dayosizi ya mpingo wakotolika ya Mzuzu awalimbikitsa kuti azikhala otanganidwa ndi nkhani zotukula mpingo-wu mdziko muno. Bambo mlangizi wa achinyamata mu parish-yi bambo Samuel Nawasha anena izi loweruka pa bwalo la za masewero la St. Augustine pomwe achinyamata kuchokera mma zoni onse anayi a mparishi-yi anakumana malo amodzi ndi kuchita masewero olimbitsa thupi monga mpira ndi zina zambiri. Iwo anati ndondomekoyi inakhazikitsidwa ndi ambuye John Ryan omwe ndi episkopi wa dayosiziyi ndi cholinga chofuna kulimbikitsa achinyamata kuti azikhala otanganidwa ndi zinthu zina pofuna kupewa makhalidwe oyipa omwe angamachite kaamba kosowa zochita. Program imeneyi muyambitsi weniweni ndi ambuye Ryan omwe ndi mwini wake wa dayosizi ino pofuna kuwapatsa chisamaliro chapadera pa moyo wawo wauzimu komanso wa wa thupi, anatero bambo Nawasha. Mmau ake mmodzi mwa achinyamata omwe anachita bwino pa zamasewerowo Jonas Muhango anayamikira dayosiziyo kamba ka chikonzerochi zomwe iye wati zithandiza achinyamatawa kukhala ozipereka mu mpingo komanso kudziwana ndi anthu ena omwe ndi a dayosizi yomweyi koma amakhala maparish ena. Mpikisanowu uyambira mmadinale onse kenako omwe achite bwino mmadinale azakafika mpaka pa dayosizi kuti akapikisane ndi achinyamata a madinale ena. ",16 " Alangiza boma pa kayendetsedwe ka chuma Adadza ndi ndondomeko: Gondwe Zipani zotsutsa boma ndi akatswiri pa kayendetsedwe kabwino ka boma ati boma lisamale kwambiri mmene liyendetsere ndalama zapadera zomwe aphungu a Nyumba ya Malamulo adavomereza boma kugwiritsa ntchito kwa 4 ikudzayi. Nyumba ya malamulo idavomereza boma kugwiritsa ntchito ndalama zokwana K210 biliyoni Lachisanu sabata yatha koma otsutsa ndi akatswiri ati kusowa kwa ndondomeko yeniyeni ya mmene ndalamazi zigwirire ntchito ndi nyambo. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Wolankhulira chipani cha Malawi Congress Party (MCP) pankhani za chuma mNyumba ya Malamulo Joseph Njobvuyalema adati kunena kuti boma igwiritsa ntchito ndalamazi si ndondomeko ya chuma cha dziko choncho nkofunika kusamala mmene zigwiritsidwire ntchito. Ndondomeko yeniyeni ya chuma cha dziko imafotokoza bwinobwino mmene ndalama iliyonse igwirire ntchito kotero kumakhala kosavuta kulondoloza pomwe ndalama izi nzongofuna kukokera boma pomwe ndondomeko yeniyeni ikubwera, adatero Njobvuyalema. Iye adati pachifukwachi boma likufunika kuonetsetsa kuti ndalamazi zagwira ntchito moyenerera makamaka mnthambi zofunika kwambiri za boma. Wolankhulira chipani cha Peoples Party (PP) Ralph Jooma adati nduna ya zachuma Goodal Gondwe amayenera kulongosola mmene nthambi za boma zipindulire ku ndalamazi kuopa mchitidwe osakaza. Akatswiri pa zakayendetsedwe kabwino ka boma ayamikira Nyumba ya Malamulo povomereza ndalama zapaderazi koma ati zonse zili mmanja mwa boma kuonetsetsa kuti ndalamazi zapindulira Amalawi. Mkulu wa bungwe la mpingo wa Chikatolika lowona kuti boma likuyendetsedwa mwachilungamo ndi mtendere la Catholic Commission for Justice and Peace (CCJP), Chris Chisoni, wati K210 biliyoni ndi yokwana kupindulira boma ngati zitagwiritsidwa bwino ntchito. Malamulo a dziko lino amapereka mphamvu kuboma kupempha ndalama zapadera ngati mboma mulibe ndalama koma chofunika ndi chilungamo kuti eni ndalamazo, omwe ndi Amalawi, apindule nazo, adatero Chisoni. Gondwe adauza Nyumba ya Malamulo Lachisanu sabata yatha kuti boma la DPP lidapeza mboma mulibe ndalama pomwe limatenga boma ndipo kuti boma lapitalo lidasiya ngongole zankhaninkhani zofunika kubweza. Nkhawa ya zipani zotsutsa ndi akatswiri ndi mchitidwe osolola ndalama za boma omwe udachititsa kuti maiko omwe amathandiza dziko la Malawi anyanyale ndi kuimika thandizo lawo. Mkulu wa bungwe la Institute for Policy Interaction (IPI) Rafiq Hajat adati kuima kwa thandizo lochoka kunja kumaimitsa ntchito zina zaboma ndipo anthu amavutika. ",2 " Njala ikhaulitsa a Malawi Ma Admarc ena kuli gwagwagwa! Zafika pena. Ngati wina samwalira ndi njala ungokhala mwayi chabe koma zinthu zaipa mdziko muno moti anthu ena akugona kumimba kuli pululu. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika akunenetsa kuti palibe amene amwalire ndi njala, koma ngati sipachitika china chake mmisika ya Admarc mdziko muno ena amwalira nayo. Mzere wa ofuna kugula chimanga ku Admarc Ulendo wa Tamvani mmaboma a chigawo cha kummwera, pakati komanso kumpoto, wapeza kuti madera ena patha miyezi ingapo chimanga chikusowa mmisika ya Admarc. Ma Admarc a Chikomwe, Ngwerero, Nasawa, Mayaka, Sunuzi, Jenala, Zaone ndi Buleya mboma la Zomba kwa T/A Mbiza akuti atha miyezi iwiri kulibe chimanga. Gulupu Belo wati malinga ndi kusowa kwa chimangacho, anthu amagonera deya amene amagula pamtengo wa K240 pa kilogalamu. Panopa amene wapeza gaga ndi munthu. Chakudya chasowa, moti ndatumiza anthu 8 kuchipatala amene amaonetsa zizindikiro zachilendo chifukwa chosadya, adatero Belo. Ku Mwanza malinga ndi T/A Kanduku, miyezi iwiri yatha chimanga kulibe. Iye wati poyamba anthu amagonera mango koma lero ndiye kolowera kwasowa. Ndi nkhani yosabisa, njala yavuta kuno ndipo chimanga chatenga nthawi chisadafike ku Admarc, adatero Kanduku. Ku Balaka patha miyezi iwiri chimanga chisadafike pa Admarc ya Phalula pamene kwa Sosola ndiye patha mwezi. Sabata yatha tidapeza anthu ammudzimo akupita kukadandaula kwa DC wa bomalo chifukwa akhala akuuzidwa kuti chimanga chibwera koma kuli chuuu. Admarc ya Misuku ku Chitipa ikumalandira chimanga mwezi ulionse kamodzi koma chimangacho chikuchokera kubungwe la World Vision. Admarc ya Chikwera mbomalo ilibiletu chimanga, pamene Admarc ya paboma yangolandira kumene matumba 300. Mabanja 2 000 ndiwo amadalira Admarc ya pabomayo koma ikugulitsa makilogalamu osaposa 15 kwa aliyense. Admarc ya pa Karonga boma ili ndi chimanga koma pamene timafikapo Lachiwiri msabatayi nkuti pali mnzere wotalika ndi mamita 280. Anthu akumagona pomwepo kuti agule chimanga. Ma Admarc a boma la Nkhata Bay akuti akumalandira chimanga pafupipafupi koma chikumatha tsiku lomwelo chifukwa chikumafika chochepa kuyerekeza ndi anthu amene akufuna chakudyacho. Mkulu wa bungwe la Admarc Foster Mulumbe wati chiyambireni September chaka chatha agulitsa matani 26 000 a chimanga. Iye watinso kufika pano, Admarc yatsala ndi matani ochepa. Chimanga chidakalipo koma chochepera, ndipo tikupitiriza kupereka mmisika yathu. Ngati chimanga chatha mmisika yathu, ndi bwino kutidziwitsa msanga kuti titumize china, adatero Mulumbe. Miyezi ingapo yapitayo, boma lidagula matani 30 000 a chimanga mdziko la Zambia. Woyendetsa ntchito wamkulu mu unduna wa malimidwe Bright Kumwembe wati chimanga chonsecho chidapita kumisika ya Admarc. Chimanga chonsecho chidafika mdziko muno ndipo chili mmisika ya Admarc. Likulu losamala chakudya la National Food Reserve Ageency [NFRA] likugula chimanga china mdziko momwe muno, adetro Kumwembe. Nkhani ya njala si yachilendonso mdziko muno. Bungwe la World Food Programme (WFP) lati lakwanitsa kufikira anthu 1.6 miliyoni mmaboma 15 amene ali pamoto wa njala. WFP Lolemba lidatulutsanso lipoti lina lomwe limati anthu 14 miliyoni ali pachiopsezo chokukutika ndi njala kummawa kwa Africa. Dziko la Malawi ndi limodzi mwa maiko okhudzidwa chifukwa cha mavuto a kusowa kwa mvula. ",2 "Mwana wa Dos Santos Anathawa Mlandu-Boma Mkulu woyimira boma pa mlandu mdziko la Angola wati akufuna mwana wa mtsogoleri wakale wa dzikolo Isabel Dos Santos abwelerenso mdzikolo. Malipoti awailesi ya BBC ati Santos yemwe ndi mmodzi mwa amayi olemera kwambiri kuno ku Africa, anakhazikika ku London bambo ake atangochoka pa udindo wa utsogoleri wa dzikolo. Akuti akukhudzidwa ndi katangale ku dziko la kwawo-Santos Mayiyu ati akukhudzidwa ndi nkhani za katangale zomwe zimachitika mdzikolo nthawi yomwe bombo ake anali mtsogoleri wa dziko. Polankhuklapo, Santos wati zomwe apolisiwa akunena ndi zabodza ndipo ndi ndale chabe. Mmodzi mwa apolisi azofufufzafufuza-wa Helder Pitra wauza wailesi ya dzikolo kuti ndi thandizo lochokera ku maiko a Portugal, Dubai ndi maiko ena, achita chothekera kumubweretsa Santos kumudzi kuti azayimbidwe mlandu wokhudza za katangale zomwe anachita mdzikolo. Mwazina, nkhaniyi inafika kale ku bwalo lamilandu la mdzikolo pomwe zinaululika kuti mayiyu amagwiritsa ntchito makalata achinyengo pochita malonda ake mdzikolo. ",7 " Kucheza ndi Ibu Mphanje: Gaba wochemerera Bullets Anthu otsata masewero a mpira wa miyendo alipo ambiri koma ena amaonjeza kukonda kwake. Ena adachita kufika popereka maina achilendo kumatimu omwe amachemerera ati pofuna kuwopseza anzawo. Ibu Mpanje ndi mmodzi mwa ochemerera timu ya Big Bullets yomwe eni ake amati Timu ya Fuko kapena Ma Palestina. Ndidacheza naye motere: Mphanje: Masapota tionjezera mphamvu Moni wawa komanso ndikudziweni? Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ine ndine Ibu Mpanje kwathu nku Nathenje koma ndikukhala mtauni ya Lilongwe. Ndimakonda kwambiri masewero a mpira wa miyendo moti timu yanga ndi Big Bullets. Anthu ambiri amandidziwa ndi dzina lakuti Gabadinho, osati osewera mpira uja, ayi, koma wochemerera. Tsono dzina la Gabadinho lidabwera bwanji? Basi kumpira anthu ambiri amandipatsa ulemu pa nkhani yochemerera ndiye nthawi ija kudadzatulukira Gabadinho wa mpira ija anthu amatengera momwe adagwedezera iye nkumandiitana ndi dzina lomwelo. Anthu ambiritu amakonda kudzitcha okha maina a anthu otchuka, sizili choncho ndi iwe? Ayi, nokhaso mudaona momwe zidalili kuja kokhala anthu ochemerera momwe ndidagwedezera ochemerera matimu ena omwe samafunira Bullets zabwino. Zimakhala mommuja nthawi zonse kukakhala mpira, makamaka wa Big Bullets, timu yanga kuyambira kalekale. Umangokonda mpira basi kapena uli ndi mbiri iliyonse pamasewerowa? Mpira ndinkasewera kalekale kuyambira kupulayimale mpaka mmakalabu ena ndi ena moti kusiya ndidasiyira pa timu ya KIA. Ndasewerako malo osiyanasiyana mgalaundi koma malo omwe ndidasewera kwambiri ndi kutsogolo. Kuvulala ndiko kudandichititsa kuti ndisiye kusewera mpira. Ndidavulala kamodzi ndiye kuyambira pomwepo ndinkati ndikasewera mpira ndimadzutsa vutolo. Malingaliro ako adali otani panthawiyo? Panthawiyo ndinkafunitsitsa kudzasewera mmatimu akuluakulu makamaka ya Big Bullets moti sindikaika kuti chipanda kuvulalako, nkadafika pomwe ndimafunapo. Anthu omwe adandionererako nthawi imeneyo akhoza kufotokoza bwino za luso lomwe ndidali nalo moti pano ndimadandaula kwambiri chifukwa ndidasiya mpira ndisadasewereko mutimu ya Flames. Chifundo chosechi pa timu ya Bullets bwanji supikisana nawo pamaudindo kuti uzitumikira nawo? Ayi, zinthu zimafunika kupatsana mpata. Ngati pali ena omwe aonetsa kale mtima wofuna kutumikira, ena mumafunika kuthandiza amenewo kuti pakhale umodzi chifukwa nonse mukamalimbirana, mkangano suchedwa kuyamba, ayi. Sabata yathayi mwasewera masewero awiri omwe simudapambaneko. Zikutanthauzanji kwa iwe ngati wochemerera? Poti awo adali masewero ongopimana mphamvu ndiye sindingazitengere kwenikweni, koma tikudikira ligi ikayamba ndiye anthu adzaone Bullets yeniyeni. Mudaona nokha ligi yathayo momwe Bullets idavutira, chaka chino tiposa pamenepo ndipo ifenso ochemerera tionjezera mphamvu kuti anyamata osewera nawo adzadzipereke kotheratu. ",16 " Njovu ziwiri zitengetsana pa 19 May Zadziwika tsopano kuti njovu ziwiri zomwe ndi mgwirizano wa Democratic Progressive Party (DPP) ndi United Democratic Front (UDF) komanso Malawi Congress Party (MCP) ndi UTM Party ndizo zidzalimbane pachisankho cha pa 19 May. Izi, zidatsimikizika Lachitatu zipani za MCP ndi UTM zitabwera poyera nkunena kuti mgwirizano wawo womwe wakhala mphekesera chabe kwa nthawi yaitali tsopano watheka. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Izi zikutanthauza kuti tsopano zipani zinayi zomwe zidali zikuluzikulu pachisankho cha pa 21 May chaka chatha tsopano zapanga mbali ziwiri zomwe zidzapikisane pachisankho chomwe chikubwerachi. Zipani za DPP ndi UDF zidalengeza mgwirizano wawo pa 25 February pomwe MCP ndi UTM ati mgwirizano wawo wangopsa kumene ndipo adzasainira pa 19 March ku Bingu International Convention Centre (BICC) ku Lilongwe. Polengeza mgwirizano wawo, DPP ndi UDF onse adati adaona kuti mfundo zawo zachitukuko ndi zolinga zawo nzofanana ndipo MCP ndi UTM nawo akunena zomwezo. Migwirizanoyi yapangidwa pokonzekera chisankho cha mtsogoleri wa dziko lino chobwereza potsatira chigamulo cha Constitutional Court choti chisankho cha pa 21 May sichidayende bwino ndipo chibwerezedwe. Khothilo lidagamula kuti chisankhocho chichitike mmasiku 150 kuchokera pa 3 February 2020 pomwe lidapereka chigamulo chake chomwe chidakomera Lazarus Chakwera wa MCP ndi Saulos Chilima wa UTM Party. Awiriwa adakamangala kukhoti kuti bungwe loyendetsa chisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) lidapotoza zotsatira zachisankhocho chomwe lidapambanitsa Peter Mutharika wa DPP. Koma zokonzekera chisankhocho ziyembekeza kuti mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika asainire mabilo a zachisankho amene aphungu a Nyumba ya Malamulo adapereka kwa iye. Mwa zina, mabilowo akuti chisankho cha aphungu ndi makhansala chotsatira chidzachitike mu 2025 kuti chidzalingane ndi cha mtsogoleri wa dziko lino. Aphunguwo adapemphanso Mutharika kuti achotse makomishona a MEC amene bwalo lidawapeza kuti sadayendetse bwino chisankho cha pa 21 May chaka chatha. Oimira ufulu wa anthu Timothy Mtambo, Gift Trapence ndi MacDonald Sembereka adamangidwa pokonza zionetsero zokakamiza Mutharika kuchotsa makomishonawo. Wotambasula za ndale Humphreys Mvula wati polingalira za nthawi yomwe yatsala kuti chisankho chichitike, nkoyenera kuti Pulezidenti asadikire masiku 21 kuti asayinire mabiluwo. Nzoona malamulowo akutero koma apapa tikuyangana nthawi yomwe ilipo kuti chisankho chichitike, adatero iye. ",11 "Bambo Stanislaus Chinguwo Amwalira Mwambo woyika mmanda thupi la malemu bambo Stanislaus Chinguwo, uchitika loweruka likudzali pa 30 May, 2020 ku Limbe Cathedral mu arkidayosizi ya Blantyre. Malemu bambo Chinguwo Bambo Chinguwo amwalira mbandakucha wa lero lachinayi pa 28 May, 2020 ku chipatala cha Mwaiwathu mu mzinda wa Blantyre. Mwambo wa maliro ukuyembekezeka kudzayamba 10 koloko mmawa, motsogozedwa ndi arkiepiskopi wa arkidayosiziyo Ambuye Thomas Luke Msusa, omwenso ndi wapampando wa bungwe la maepiskopi a mpingo wa katolika mdziko muno la Episcopal Conference of Malawi (ECM). Chikalata chomwe likulu la mpingo wa katolika latulutsa chati mawa sikukhala kusonkhana ndi kuchita mapemphero ndipo mmalo mwake ansembe komanso akhristu akupemphedwa kuti adzipemphelera malemu bambo Chinguwo mmakomo mwawo kuti mzimu wawo uwuse mu mtendere. Malemu bambo Stanislaus Chinguwo anabadwa pa 19 January mchaka cha 1969 ndipo amachokera ku Namlenga parish mu arkidayosiziyo. ",14 " Akulipitsa kulembetsa khadi Anthu ena amene sadalembetse nambala zawo akulirira kuutsi pamene ma agenti ena akuwauza kuti alipire ngati akufuna nambala yawo ilembetsedwe. Izi zikudza pamene makampani a foni za mmanja a Airtel ndi TNM adachotsa nambala zimene sizidalembetse pofika pa 30 September chaka chino. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Kulembetsa makadi ndi kwa ulere Ngakhale kampanizi zidachotsa nambala zina, eni nambalawo ali ndi mwayi wokalembetsa nthawi iliyonse mwaulere. Koma izi zikusiyana ndi zimene anthu ena akukumananazo pamene akupemphedwa kulipira kuti nambala yawo ilembetsedwe. Mboma la Mulanje ndi Thyolo anthu ena akulipira kuti alembetse nambala zawo. Mtolankhaniyu atayendera malo ena ku Chirimba mafupi ndi sitolo ya Macsteel adauzidwa kuti alipire K300 kuti nambala yake ya Airtel ilembetsedwe. Tikuyenera tigule mayunitsi a K300 omwe timalowera mu system ya Airtel kuti nambala yanu ilembetsedwe. Koma nambala yanuyo idadulidwa mwezi wapitawo zomwe zimapangitsa kuti ntchito yathu ikhale yovuta, adatero agentiyo. Titamuuza kuti tili ndi K100, iye adakananso kuti ndalamayo yachepa chifuwa polingalira kukula kwa ntchito yolumikizira nambalayo. Mneneri wa kampani ya Airtel Norah Chavula-Chirwa adati ndi wodzidzimuka kuti anthu ena apezerapo mwayi kumabera makasitomala awo pamene akulembetsa nambala zawo. Iye adati kampani yawo iyesetsa kuyenda mmidzi kulangiza anthu kuti sakuyenera kulipira polembetsa nambala. Tikulangiza makasitomala athu kuti aimbe 121 ngati wina wawauza kuti alipire polembetsa nambala yawo. Ngatinso mderalo kuli ofesi yathu, athamangireko kuwamuneneza agent amene akulipiritsayo. Apo ayi athamangire kupolisi kukanena. Pamene akuimba 121, ayenera adziwe code ya agent-yo kuti tichotse nambala yake, adatero Chirwa. Naye mneneri wa kampani ya TNM, Daniel Makata adati alandira nkhani zotere mboma la Mulanje komwe agent akufuna ndalama kuti alembe nambala. Makata adati kampani yawo idalemba ntchito ma agent oposa 2500 mmadera onse a dziko lino kuti alembe onse amene ali panetiweki ya TNM. Ifeyo tidawalemba ntchito, ndi kulakwa kuti nawonso ayambe kulipiritsa makasitomala athu. Anthu adziwe kuti kulembetsa nambala ndi kwaulerere, sakuyenera kulipira kanthu pa ntchito imeneyi. Ngati wina wakupemphani ndalama chonde tidziwitseni apo ayi pitani kupolisi, adatero Makata. Makata adati pofika pa 30 September, kampani yawo nkuti italemba makasitomala 75 pa 100 alionse. ",11 "Papa Wasankha Mkulu Woona Zachuma ku Vatican Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wasankha mkulu wa bungwe loyangana momwe chuma chiyendera ku likulu la mpingo ku Vatican. Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican Papa Francisco wasankha Giuseppe Schlitzer kulowa mmalo mwa Tommaso Di Russa yemwe nthawi yake yokhalira pa udindowu inatha mwezi wa January chaka chonchino. Likulu la Mpingo wa Katolika ku Vatican lalengeza za kusankhidwa kwa akuluakulu awiri oyanganira bungwe la Mpingowu loona momwe chuma chiyendera. Mkulu wa bungweli lomwe limadziwika pa chingerezi kuti Financial Intelligence Authority ndi Giuseppe Schlitzer ndipo womutsatira wake ndi Federico Antellini Russo. Awiriwa akulowa mmalo mwa Tommaso Di Russa yemwe adatsiriza ntchito yake pa 20 January chaka chonchino atakhala pa udindowu kwa zaka zisanu. Mwa zina bungweli limalimbana ndi machitidwe wozembetsa ndalama (money laundering). Papa Benedicto wa 16 ndiyemwe adakhazikitsa bungwe la Financial Intelligence Authority mchaka cha 2010 kuti liziona momwe ndalama zimagwiritsidwira ntchito ku likulu la Mpingo ku Vatican komanso kuti ndondomeko za chuma zomwe likulu la Mpingo wa Katolika limatsata nzogwirizana ndi momwe mabungwe komanso maiko achitira. ",14 " Anthu 50 000 akutenga HIV chaka chilichonse Pamene nkhondo yolimbana ndi matenda a Edzi ikupitirira, zadziwika kuti chaka chilichonse anthu 50 000 akutenga kachirombo ka HIV kamene kamayambitsa matendawa. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Polankhula pamwambo woganizira anthu amene adataya miyoyo yawo kaamba ka nthendayi komanso amene ali ndi kachirombo koyambitsa nthendayi, wachiwiri kwa pulezidenti wa dziko lino Khumbo Kachali adati aliyense ayenera kutengapo gawo kuti chiwerengerochi chitsike. Ndi udindo wa tonse kulimbana ndi matenda a Edzi ndipo tonse tiyenera kuyezetsa, adatero Kachali, yemwenso ndi nduna ya zaumoyo. Mkulu wa bungwe la UNAIDS ku Malawi Patrick Brenny adati Malawi ikuchita bwino pankhondo yolimbana ndi matendawa. Malawi akuchita bwino makamaka makamaka pankhani ya kadyedwe, kuchepetsa kupatsirana kwa nthendayi pakati pa mayi ndi mwana komanso ma ARV, adatero iye. Koma Brenny adati nkofunika kuti Amalawi agwirane manja ndipo asatope popewa matendawa. Pamwambowo, wogwira ntchito kuwailesi Wesely Kumwenda adati atolankhani amene adapezeka ndi HIV ayenera kubwera poyera. Iye adati ngakhale adamupeza ndi HIV zaka 10 zapitazo, alibe nkhawa, ndipo wabereka ana awiri pakatipa. ",6 " Kuweta ngombe zamkaka nkokoma, koma. Alimi ndi akadaulo ena pa zaulimi abwekera ubwino ndi phindu la ulimi wa ngombe, koma ati pali zina zoyenera kuchita kuti ulimiwu ufikepo. Mwa zina, ngakhale alimi ambiri amene adacheza ndi Uchikumbe mzigawo zonse za dziko lino adati akusimba lokoma paulimiwu pali zina zoyenera kukonza kuti phindulo libwere pambalambanda. Kadaulo pa nkhani ya ziweto kusukulu ya ukachenjede ya Lilongwe University of Agriculture and Natural Resources (Luanar) pulofesa Timothy Gondwe komanso mkulu wa mgwirizano wa mabungwe okhudzidwa ndi ulimi la Civil Society Agriculture Network (CisaNet) a Tamani Nkhono-Mvula adaphera mphongo zonena za alimiwo. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu A Gondwe adati pakadalipano alimi a ngombe zamkaka akuchuluka koma chiwerengero cha ngombe nchochepa. Pali zina zoyenera kusintha kuti alimi a mkaka apindule kwambiri Iye adati izi zili choncho chifukwa ambiri mwa iwo ndi angonoangono ndipo amakhala ndi ngombe imodzi kapena ziwiri. Alimi akuluakulu sakuonetsa chidwi ndi ulimiwu. Alimi aangono ambiri alibe zipangizo komanso akusowa ulangizi pa kadyetsedwe, kasamalidwe ka ngombe komanso momwe angasamalire mkaka wawo kuti ukapeze msika wabwino, adatero Gondwe. Adapereka chitsanzo cha ngombe ya mkaka ya mtundu wa Fresian imene itadyetsedwa bwino ikhoza kutulutsa malita 40 pa tsiku koma alimi ambiri amakama malita 10 kapena 12 okha patsiku. Iwo adatinso vuto lina ndi ndondomeko zoyendetsera msika wa mkaka. Pophera mphongo, Nkhono-Mvula adati imodzi mwa ndondomeko zimene zimathimba alimiwa pakhosi ndi Gawo 36 ya malamulo a bizinesi ya mkaka. Malingana ndi lamuloli, alimi angonoangono sangagulitse mkaka wawo momasuka pokhapokha atakhala ndi njira zowiritsira yomwe ndi ntchito ina yapadera chifukwa afuna kudutsa mndondomeko zambiri kuti avomerezedwe kutero. Pachifukwa ichi, alimiwa amakakamizidwa kukagulitsa mkaka wawo kumakampani omwe ali ndi zipangizo pamtengo wozizira, adatero iwo. Malinga ndi mkuluyo, alimi a mkaka ali pachipsinjo cha misonkho kusiyana ndi alimi ena poti iwo amadulidwa msonkho pa ndalama zilizonse zomwe angapate pa malonda awo pomwe pamalamulo a msonkho, munthu amayenera kudulidwa msonkho ngati wapeza ndalama zoposa K50 000 pa mwezi. Mawu a akadaulowa akungopherezera zimene alimi ena mzigawo zonse zitatu adauza Uchikumbe. Wapampando wa gulu la Lusangazi Dairy Farmers Cooperative ku Mzimba, Hesco Banda, adati vuto la kusowa kwa zakudya likuchititsa miyoyo ya alimiwa kukhala yowawa. Iye adati ngakhale alimi ali ndi kuthekera kogula chakudya cha ngombezo pamtengo wa K10 000 thumba la makilogalamu 50, chikusowa. Zakudya zikusowa, moti tikungogwiritsa ntchito deya. Vuto lake, deyayu tikulimbirananso ndi anzathu a ku Tanzania amene akulolera kugula deyayo pamtengo wa K500 pa kilo mmalo mwa mtengo wake wa K200, adandaula Banda. Vuto lina, iye adati, ndi kusowa kwa msika chifukwa kumpoto kulibe kampani zogula mkaka monga momwe zilili mzigawo zina. Kampani za Lilongwe Dairy, Suncrest Creameries komanso Dairibord zimagula mkaka kumwera ndi pakati. Adaonjeza kuti izi zachititsa kuti mavenda alowererepo, pomagula mkaka pamtengo wolira. Ngakhale msika ulipo, alimi ena, monga Thomson Jumbe wa mmudzi mwa Waruna, T/A Chimaliro ku Thyolo mitengo ndiyotsika. Malingana ndi unduna wa malimidwe, mtengo wotsikitsitsa umene mkaka uyenera kugulitsidwira ndi K155 pa lita. Timagulitsa mkaka pa mtengo wa K150 pa lita pomwe kuti titulutse lita imodzi zimalowa ndi zambiri, makamaka tikawerengera zakudya monga deya komanso mankhwala, adatero Jumbe. Poyankhapo pamadandaulowa, nduna ya zamalimidwe ulimi wothirira ndi chitukuko cha madzi Dr George Chaponda adati unduna wake uunika madandaulowa nkuwona kuti ungathandizane bwanji ndi alimiwa kuti ulimiwu upite patsogolo. ",4 "Chipatala cha Kamuzu Central Chayika Ndondomeko Zatsopano Zopewera COVID-19 Akuluakulu a chipatala cha Kamuzu Central mu mzinda wa Lilongwe ayika ndondomeko zatsopano ngati njira imodzi yofuna kuteteza anthu odwala ku mliri wa COVID-19 pa chipatalachi. Anthu akamalowa apa aziyamba ayezedwa Izi zadziwika kudzera mu chikalata chomwe akuluakulu a pa chipatalachi atulutsa chomwe chikufotokoza ndondomeko zatsopano zomwe akhazikitsa zopewera mliri-wu. Mwazina chipatalachi chati chiziwonetsetsa kuti aliyense wolowa mzipata za pa chipatalachi akuyezedwa ku nthendayi. Tikufuna tichepetse kuchuluka kwa anthu omwe amabwera kuzaona odwala, kudzadikilira odwala. Tichepetsanso magulu amene amabwera kuzachita za tchalitichi ndi mapemphero mu ward zomwenso zimachititsa kuti anthu achulukane ndi kufalitsa matendawa, anatero a Kambeni omwe ndi mmodzi mwa akuluakulu a pa chipatalachi. Kudzera mu kalatayi chipatalachi chati anthu opita ku chipatalachi adzivala face mask, adzisamba mmanja komanso aziyezedwa mu zipata zolowera ku chipatalachi. ",6 " A khonsolo ndi ankhanzaAmalonda Ena mwa ochita malonda (mavenda) mmisewu ya mumzinda wa Blantyre alira ndi khalidwe la akhonsolo ya mzindawu kuti akuwachitira nkhanza ngati Malawi si dziko lawo. Pocheza ndi Msangulutso mavendawa akuti akupempha khonsoloyi kuti iwaganizire, maka iwo amene akuchita mabizinesi angonoangono. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Koma mneneri wa khonsoloyi, Anthony Kasunda, akuti sadalandirepo dandaulo lililonse kuchokera kwa anthuwa. Iye wati zomwe akudziwa nzoti akhonsolowa akumamenyedwa ndi mavenda akamagwira ntchito yawo yoletsa malonda mmalo amene si oyenera kuchitiramo bizinesi. Tikudziwa kuti nthawi zambiri ma rangers (othamangitsa anthu mmalo oletsedwa) athu akhala akugendedwa ndi mavenda ndipo umboni ulipo chifukwa timapita nawo kuchipatala. Galimoto zathunso zagendedwapo kambirimbiri. Mukumbukira kuti ranger wathu wachikazi adamenyedwa mu Limbe ndi ochita malonda koma anthu anaona ngati kuti wamenyedwa ndi venda, adatero Kasunda. Komabe amalondawa akuti akhala akudandaulira khonsoloyi koma sichitapo kanthu. Francis James, amene amagulitsa mkaka wamadzi wa mmapaketi) adati adamenyedwapo ndi akhonsolowa komanso kumulipitsa K5 000 kaamba kochita malonda mumzindawu. Adandigwira madzulo ndikupita kunyumba. Mmanja mwanga ndidali ndi machubu awiri a mkaka. Adandigwira ndi kundimenya ndi zitsulo mmiyendomu ndipo adandilipiritsa K5 000, adatero James. Iye akuti akukumbukiranso za mnzake wina amene ankagulitsa nsapato. Adamulanda nsapato zonse ndipo patadutsa sabata, tidakumana ndi mmodzi mwa amene adamulandawo atavala imodzi mwa nsapatozo. Mnzanga wina wogulitsa maheu adamumenyanso ndi zitsulo komanso adamumwera maheuwo, adatero James. Naye mayi wina, yemwe adati ndi Alinafe, akuti adamugwira ndipo adakamutsitsa ku Chileka kuti akayende wapansi kuchokera kumeneko atamugwira ndi malonda a nthochi. Koma Kasunda akuti katundu aliyense akuyenera kugulitsidwa mmalo ovomerezedwa ndi khonsolo kukhala msika. Malo oyenera kuchita malonda ndi okhawo omwe khonsolo idakhazikitsa ngati msika, komanso malo amene avomerezedwa ndi khonsolo potsatira pempho lochokera kwa ofuna kuchita malonda. Dziwani kuti aliyense wochita malonda malo amene khonsolo lavomereza amakhala ndi chiphaso, adatero Kasunda. ",2 " Ndale zogawanitsa miyambo zanyanya Si zachilendonso kumva kuti andale adzetsa ziwawa pamwambo wachikhalidwe. Lamulungu, kudali gwiragwira kokhazikitsa mwambo wag ulu la Ayao lomwe likutchedwa Chiwanja Cha Ayao. Pamwambowo, wothandizira wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Saulos Chilima adamunjata pomuganizira kuti amachita zokaikitsa. CSOs in Pay Back Our Money campaign Govt to review Genset deal Govt moves to audit firearms Othandizira Chilima (pakati) adamangidwa pochita zokaikitsa Anthuwo ati adali ndi mphatso yochoka kwa Chilima koma adalephera kupereka chifukwa cha zovuta zina. Izi zimachitika patangotha mwezi, patabukanso chisokonezo pamaliro a Themba la Mathemba Chikulamayembe mboma la Rumphi. Mpungwepungwe udadza pamene ampingo adalandidwa chimkuzamawu pamene amapereka mpata kwa Chilima ndi mtsogoleri wa zipani zotsutsa Lazarus Chakwera kuti alankhule. Nakonso ku mwambo wa Gonapamuhanya wa Atumbuka kwakhala kukuchitika zisokonezo zodza ndi andale kwa zaka ziwiri zotsatizana. Mmalo mopitira zomwe ayitanidwira, andalewo amafuna kupikisana ku miyamboyo ndipo salola kugonjerana. Polankhulapo pa mchitidwewo, kadaulo wa ndale pa sukulu ya ukachenjede ya University of Livingstonia George Phiri adati vuto lalikulu limabwera chifukwa okonza miyamboyo amapereka gawo lalikulu kwa andale. Phiri adapereka chitsanzo cha mwambo wa kulamba omwe Achewa amakonza mdziko la Zambia komwe ngakhale kumapita andale, sapatsidwa mphanvu. Iye adati izi zimathandiza kuti kumaloko kusakhale mpikisano ndi kudzionetsera pakati pa zipani. Achikhalidwe azionetsetsa kuti mwambowo uli mmanja mwawo osati kuwapatsa andale, adalongosola Phiri. Iye adatinso vuto lina limadza maka andalewo akatenga gawo lalikulu popereka thandizo lokonzera mwambo wa mtunduwo. Tiyeni tisiye zomachita ndale paliponse chifukwa zikuononga chikhalidwe. Tizilekanitsa zinthuzi, adatero Phiri. Naye mbusa Macdonald Sembereka yemwe ndi mmodzi wa akuluakulu omwe adakonza mwambo wa Chiwanja cha Ayao adati vuto la andale ndi loti amafuna kudzionetsa kuti wa mkulu mndani ku miyambo yachikhalidwe. Sembereka adati andalewo amaphangira ku zochitikazo mpaka kuononga miyambo ya chikhalidwe. Khalidwe ili silikuthandiza chikhalidwe chathu. Tikuwapempha kuti asamapezerepo mpata wotsatsa malonda awo pa miyamboyo, adatero Sembereka. Iye adatinso andalewo ngofunika kulolerana pa nthawi ngati imeneyo ndipo adapereka chitsanzo cha mtsogoleri wopuma wa dziko lino Joyce Banda yemwe ngakhale ali wa mtundu wa Chiyao sadakhale nawo. Anthufe tikungoyenera kudziwa kuti chikhalidwe nchachikulu kuposa ndale ndipo ndale zikufunika kulamulilidwa ndi chikhalidwe, adatero Sembereka. Wapampando wa gulu losunga chikhalidwe cha Achewa, Kanyama Phiri adati gululo limakana kutengapo gawo pa ndale chifukwa malamulo awo ochokera kwa Gawa Undi sawavomereza kutero. Phiri adati popewa andale kuwasokonezera zachikhalidwe chawo, gululo amakakumana kwa Gawa Undi basi. Palibe cholakwika kuwaitana andalewo koma mpofunika kukhazikitsa ndondomeko zoti azitsatira akafika pamalowo, adatero Phiri. Naye Gogo Chikalamba Gondwe yemwe amakonza mwambo wa Atumbuka wa Gonapamuhanya omwe wakhala ukukumana ndi mazangazime chifukwa cha andale, adati gulu lawo tsopano lidaika ndondomeko zomwe andalewo amatsatira popewa chisokonezo. Komabe tinene kuti nthawi zambiri tikayandikira nthawi yosankha atsogoleri, andalewo amalowerera ndithu cholinga choti anthu awadziwe, adatero Gondwe. Iye adati gulu lake lidawauza andalewo kuti akamapita ku mwambo wa Gonapamuhanya, azikangoonera osati kuchitapo ndale. ",11 " Amayi omwe ali ndi kachilombo akufuna mudzi wawo Amayi omwe ali ndi kachilombo koyambitsa matenda a Edzi ka HIV kwa T/A Kalolo ku Lilongwe apempha boma kuti liwapatse mudzi wawo kuti azipindula nawo pa ndondomeko ya zipangizo za ulimi zotsika mtengo ya sabuside. Amayiwa ati mafumu a mmidzi yomwe akukhala amawasala mnjira zambiri kuphatikizapo pa kagawidwe ka makuponi ogulira zipangizozi zomwe zimapangitsa kuti mabanja awo azikhala ndi njala chaka ndi chaka. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Iwo adapereka pempholi pamsonkhano omwe bungwe lowona za maufulu a anthu la Centre for Human Rights and Rehabilitation (CHRR) lidakonza kumudzi wa Kalolo ku Lilongweko kuti amaiwa akumane ndi akuluakulu osiyanasiyana kuti apereke madandaulo awo pazovuta zomwe amakumana nazo. Mkulu wa gulu lina la amayi omwe ali ndi kachilombo la Kalolo Community Aids Coordinating Committee Tisauke Nazoni wati amaiwa amaphonya kamwedwe ka mankhwala obwezeretsa chitetezo mthupi, ma ARV, chifukwa chosowa chakudya zomwe zimaika miyoyo yawo pachiopsezo. Nzokhumudwitsa kuona kuti makuponi akuperekedwa kwa anthu oti ali ndi mphamvu oti akhoza kudzipezera zipangizo mosavuta koma tikati tiyesere kudandaula amati tipalamula. Ma ARV amafunika chakudya chokwanira koma nthawi zina timalephera kumwa chifukwa palibe chakudya. Timatha kukhala ndi njala kuyambira mmawa mpaka madzulo, adatero Nazoni. Koma woyendetsa ntchito zaulimi ku Chileka EPA komwe amaiwa amachokera Chrissie Chiusiwa wati pempho la amaiwo silingatheke chifukwa midzi yolandira zipangizozi imatengera malire a ma T/A omwe amapereka ndondomeko kuboma. Iye adapempha amaiwo kuti akadandaule kuofesi yoyendetsa za ulimi kapena kuofesi ya bwanamkubwa wa Lilongwe kuti akawathandize. Mfumu yaikulu Sakuzamutu idavomereza kuti mafumu angonoangono ena amachita za chinyengo, kupondereza anthu. Iye adati aitanitsa mafumu onse kuti akhale nawo pansi ndi kukambirana nawo kuti mchitidwewu uthe. Ndizachisoni chifukwa anthu ngati amenewa ndiamene boma limaganizira mmapologalamu ngati awa a sabuside tsono ngati mafumu akutenga zinthuzi ndikumagawira anthu amphamvu kale ndiye kuti tikuchitapo chiyani? Tikhala nawo pasi kuti tikonze zonse, adatero Sakuzamutu. ",6 "MBTS Ipempha Anthu Apitilize Kupereka Magazi Wolemba: Glory Kondowe uploads/2019/09/blood-donors.jpg"" alt="""" width=""530"" height=""450"" />Ena mwa anthu akupereka magazi nthawi ya mbuyomu Bungwe lotolera magazi mdziko muno la Malawi Blood Transfusion Services (MBTS) lapempha anthu mdziko muno kuti apitirize kupereka magazi ndi cholinga chofuna kupulumutsa miyoyo ya anthu ochuluka mu zipatala zosiyanasiyana. Wofalitsa nkhani za bungweli mdziko muno a Allen Kaombe anena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi. Iwo ati udindo wopereka magazi ndi wa wina aliyese ndipo anatsutsa zimene anthu ena amaganiza kuti kupereka magazi ndi ntchito ya ophunzira okhawokha a msukulu zosiyanasiyana. Mwa zina a Kaombe ayamikira anthu omwe amadzipereka popereka magazi ku ma ofesi awo zomwe ati ndi zofunika kwambiri. Iwo akumbutsa a Malawi kuti anthu omwe akuyenera kupereka magazi ndi aliyense oyambira zaka 15 zakubadwa kulekeza 65 ndipo ndi anthanzi. Sizoti ndi ana a sukulu wokha ayi ndipo ndikupempha a Malawi onse kuti ndi udindo wawo kupereka magazi ku bungweri, anatero a kaombe. Iwo ati magazi omwe amafunikira mdziko muno ndi 120 thousand litres pa chaka ndipo amene latolera ndi 58 thousand yomwe ndi 50 percent yokha basi. ",6 "Kwaya ya Masiphumelere Ichita Ubale ndi Abwenzi a Tchalitchi la Kankhomba Kwaya yopangidwa ndi akhristu a mpingo wakatolika a kuno ku Malawi koma akukhalira ku Capetown mdziko la South Africa ya Fishhoek Masiphumelere yayamikira ubale wabwino umene ulipo pakati pa kwayayi ndi bungwe la abwenzi a tchalichi la Kankhomba mu parish ya Thunga mu arch-dayosizi ya Blantyre, koma akukhalira mdziko lomwelo la South Africa. Wapampando wa kwaya-yi a Mosses Lusale ndi omwe anena izi pakutha pa mwambo wa Paper Sunday yomwe kwayayi inachita ngati njira imodzi yofuna kupeza thandizo la ndalama zojambulira chimbale chawo. Iwo ayamikira mamembala bungwe la abwenzi a tchalichi la Kankhomba omwe akukhalira ku Capetown mdziko-mo kaamba kofika ndi kudzawathandiza pa mwambo-wu. Pamenepa a Lusale ati zomwe zachitikazi zasonyeza umodzi umene ulipo pakati pa magulu awiri-wa. Polankhulanso mmodzi mwa mamembala a bungwe la abwenzi atchalichi la Kankhomba mu parish ya Thunga mu arch-dayosizi ya Blantyre okhalira mdziko la South Africa-wa a Velonica Makawa, ati ndi wokondwa ndi ubale-wu. ",13 " Kusamvetsetsana kwabuka ku Mwanza Kusamvetsetsana kwabuka pakati pa anthu a ku Mphete mboma la Mwanza ndi ofesi ya DC wa bomali chifukwa cha nyumba ya mphunzitsi pasukulu ya Mphete imene kampani yokonza njani ya Vale Logistics idagwetsa. Malinga ndi mlembi wakomiti yoyendetsa ntchito za pasukulu ya Mphete, Allan Gaviyawo , mchaka cha 2012 a kampani ya Vale Logistics adagwetsa nyumba ya mphunzitsi imodzi pasukulu ya Mphete chifukwa inali pamalo pomwe payenera kudutsa njanji yomwe ikudutsa mdziko muno kuchokera ku Mozambique. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Gaviyawo adati kampaniyi idalonjeza kuwapatsa anthu a mderali ndalama zokwana K1.5 miliyoni kuti amangire nyumba ina pamalo ena zomwe anthu a mderali adakana ponena kuti ndalamayi siinali yokwana kumangira nyumba ina yamakono ngati yomwe inagwetsedwayo yomwe inali mphatso kwa anthu a mderali kuchokera kubungwe la European Union. Zitachitika izo, kampaniyo idalonjeza kupereka K12.7 miliyoni yoti nyumba ina imangidwe zomwe anthuwa adagwirizana nazo popeza amayembekezera kuti ndalamayi ikanakwanira kumanga nyumba ziwiri zamakono za amphuzitsi mmalo mwa imodzi. Anthu a mderali anadabwitsika poona kuti ndalamazi zinakapelekedwa kuofesi ya DC yomwe idabwera kudzamanga nyumbayo ndipo anthu aku Mphete sakukhutisidwa ndi nyumba yomwe ofesi ya DC wa boma la Mwanza yamanga pasukulu ya Mphete pakuyerekeza ndi ndalama yomwe idaperekedwa yomangira nyumbayi, adatero iye. Wapampando wa khonsolo ya Mwanza Moses Walota adati iye ndi makhansala anzake mbomali atakayendera nyumbayo adakhumudwa ndi momwe nyumbayo ayimangira ndipo sadakhutisidwe ndimamangidwewo. Walota wanena kuti ataona izi analembela kalata bwanankubwa wa boma la mwanza yomuunikira zolakwika zomwe mankhansalawa anapeza panyumbayi zoti zikonzedwe nyumbayi isanaperekedwe kwa anthu aku mphete mmboma la Mwanza. Koma mpaka lero kalatayo siinayankhidwe ndipo zolakwika pa nyumbayo sizinakonzedwebe. Poyankhapo pankhaniyi DC wa boma la Mwanza Gift Lappozo wavomereza kuti nzoona kuti kontilakitala yemwe adapatsidwa ntchitoyi wayithawa atagwira ntchito yosasangalatsa kumapeto kwenikweni kwantchitoyi koma bwanankubwayu adati padakalipano ofesi yake ikuunikanso bwinobwino mgwirizano omwe anagwirizana ndi kontilakitayu asanapeze wina oti amalizitse ntchitoyi Koma iye wakana kuti kontilakitayu adapatsidwa ndalama zonse zokhudza ntchitoyi koma kuti amalipidwa mzigawo akamaliza chigawo chilichonse chantchitoyi moyenerera. Lapozo adati kusamvetsetsana komwe kulipo pakati pa ofesi yake ndi anthu aku Mphete kwadza chifukwa cha kusadziwa momwe ofesi ya bwanankubwa imachitira pogwira ntchito ngati zimenezi komwe anthuwa alinako ndiponso chifukwa chokuti anthuwosakufuna kumva kufotokoza komwe akhala akufotokzeredwa ndi ofesi ya DC pazankhaniyi. ",7 " Samalani maso popewa khungu Khungu ndi amodzi mwa matenda a maso opeweka. Katswiri wa maso pa chipatala cha Chiradzlu Frank Mwamadi wati izi zimachitika munthu akasamalira bwino maso ake. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Iye adati munthu wakhungu ndi amene maso ake onse sakuona. Mwamadi: Khungu ndi lopeweka Khungu limadza mwadzidzidzi kapena pangonopangono, adatero mkuluyu. Mwamadi adati khungu ndi amodzi mwa matenda omwe amabwezera mmbuyo chitukuku cha munthu. Munthu wakhungu amakanika kugwira ntchito, kupanga maphunziro, kuyenda, komanso kusonkhana ndi anzake pa zochitika zosiyanasiyana, adatero katswiriyu. Ngakhale khungu ndi loopsa, katswiriyu watsindika kuti pali kuthekera kothana nalo kuti asayale maziko pa moyo wa munthu. Iye adapereka chitsanzo monga kuyezetsa maso pafupipafupi ku chipatala, kupereka zakudya za Vitamini A kwa ana, komanso kuchita ukhondo. Pamene ana akupatsidwa Vitamini A wokwanira anthu akuluakulu akuyenera kuchititsa opaleshoni diso kapena maso awo akapanga ngala chifukwa imaika maso pa chiopsezo cha khungu, adatero katswiriyu. Mwamadi adalangiza anthu kuti pamene akukumana ndi vuto la maso azithamangira ku chipatala osati kugwiritsa ntchito mankhwala azitsamba. ",6 " Mawu a JB ndi loto Akuluakulu a mabungwe ena ati mawu a mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda potsegulira msonkhano wa aphungu Lachisanu lapitalo ndi loto la chumba chifukwa ngakhale adapereka chiyembekezo kwa Amalawi, zinthu zikupitirira kuthina. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Izi zadza chifukwa patangotha maola ochepa Banda atangopereka uthenga wa chikhulupiriro ndi chiyembekezo kuti zonse ziyenda, mtengo wamafuta udakwera pomwe bungwe loona za mafuta la Malawi Energy Regulatory Authority (Mera) lidalengeza kuti petulo wakwera kuchoka pa K606.30 kufika pa K704.30 pomwe dizilo adafika pa K683.60 kuchoka pa K597.40. Malinga ndi mkulu wa bungwe la ogula la Consumers Association of Malawi (Cama) John Kapito kukwerako kukutanthauza kuti zinthu zikweranso mitengo ndipo Amalawi afinyika, kuphwetseratu chiyembekezo chimene Banda adapereka. Iye adati Amalawi akuyenera kudikira zaka 15 kapena 20 zikubwerazo kuti mfundo zomwe Banda adalankhula zidzayambe kupindulira anthu. Adangochekenira chifukwa izi ndizo akhala akuzinena. Zangosonyezeratu manthu wamavuto. Akungonena loto chabe koma osati Amalawi angayembekezerepo kanthu. Zambiri akukamba monga za Kayerekera sizingapindulire munthu wakumudzi panopa. Chiyembekezo chingabwere ngati pali njira zopindulira Amalawi monga za ntchito zomwe anthu amagwira kumudzi komanso mfundo zotukulira anthuwo koma zomwe zilipo ndikungosangalatsa omvera, adatero Kapito yemwe adati uthengawo udali wa ndale chabe. T/A Mphuka wa mboma la Thyolo adati padakali pano anthu mdera lake komanso madera ambiri mdziko muno akupanidwa malinga ndi mavuto ambiri, kuphatikizapo kukwera mtengo kwa mafuta kwa posachedwapa. Padakali pano zinthu zina zayamba kale kukwera mtengo. Koma pa mawu a Banda, sindinganenepo kanthu chifukwa ndikudziwa kuti monga mtsogoleri wa dziko lino amaona zapatali choncho mavuto amene alipo panopa akhoza kutha monga akunenera, adatero Mphuka. Ndipo mkulu wa bungwe loona kuti nkhani zachuma zikuyenda mokomera onse la Malawi Economic Justice Network (Mejn) Dalitso Kubalasa wati zomwe Banda adalankhula zakhala zikukambidwa ndi bomali ndipo wati ndibwino kulankhulaku kuthe ndipo ayambe kukwaniritsa. Uthengawu ukungofuna kuthunzitsa anthu mtima. Adanenapo kuti nduna ziziunikidwa momwe zikugwirira ntchito. Sitikudziwa ngatinso izi zili pa ndondomeko yofuna kubwezeretsa chuma cha dziko lino. Zalankhulidwa zambiri koma Amalawi akufuna zooneka kuti akhale pa mpumulo osati kungolankhula, adatero Kubalasa. Koma kadaulo wa ndale, Blessings Chinsinga adati zikukaikitsa ngati Amalawi angatonthole monga Banda adanenera muuthenga wake ponena kuti pakufunika ntchito ichitike. Iye adadzudzulanso Banda kuti palibe chomwe akuchita pofuna kukwaniritsa mfundo zokonzanso chuma cha dziko lino zomwe zili mu Economic Recovery Plan (ERP). Akuyenera kuyanganira zambiri. Sitikudziwabe yemwe akuyanganira ndondomeko ya ERP, nanga tikuchitanji kuti tifikire mlingo omwe tikufuna? Tikumvanso kuti mabilu a foni akuchita kufika mamiliyoni osaneneka. Izi zititengera nthawi kufi tifikire pachomwe tikufuna ngati dziko. Ndikaona uthengawu wangochuluka kulankhula zina zomwe akhala kale akulankhula koma chiyembekezo mulibe chifukwa anthu amadikira ntchito osati mawu, adatero Chinsinga. Masiku apitawa, kudamveka kuti nyumba ya boma kudali mabilu a foni okwana K98 miliyoni, mmiyezi 9 ndipo kampani ya mafoni ya MTL imafuna kukadula mafoni kunyumba ya bomayo. Ndipo nkhani ya mavuto a za chuma ili mkamwa, ogwira ntchito mboma Lachiwiri adayamba sitalaka yosonyeza kukwiya kwawo ndi malipiro ochepa, pamene mitengo ya zinthu ikupitirira kukwera. Iwo adatchinga zipata za kumaofesi a likulu la nthambi za boma ku Lilongwe ndipo atanyamula nthambi za mitengo adali kuimba kuti: Akulemera tikuona! Akunenepa tikuona. Malinga ndi mkulu wa bungwe la ogwira ntchito mboma la Civil Service Trade Union (CSTU) Eliah Kamphinda Banda akufuna malipiro akwere molingana ndi ogwira ntchito mmakampani. Ogwira ntchito mboma tatopa ndi kudya bonya. Sitibwerera kuntchito malire ake boma litiganizire. Boma likuchedwa dala kuti lionjezere malipiro athu ndipo tikumva kuti akweza malipiro mu Julaye ndi 5 peresenti. Sitingalole, adatero Banda. Ndipo dzulo lidali tsiku lomaliza limene bungwe la Cama lidapereka ku boma kuti likonze mfundo zina zimene amati zikulakwika mchikalata chomwe adachipereka pakutha pa zionetsero za pa 17 January. Pomwe timasindikiza, mneneri wa boma Moses Kunkuyu adati aitanitsa akuluakulu a Cama kuti akambirane. ",11 "Ogwira Ntchito Mboma Ayamba Kunyanyala Ntchito Lolemba Bungwe loyanganira anthu ogwira ntchito mboma la Civil Servants Trade Union (CSTU) lauza anthu onse ogwira ntchito mboma kuti ayambe kunyanyala ntchito kuyambira lolemba likudzali. Njolomole: Tikufuna kulikumbutsa boma zomwe tinagwirizana Mlembi wa bungweli Madalitso Njolomole wauza Radio Maria Malawi kuti iwo aganiza zochita izi kutsatira kutha kwa masiku 21 omwe anapereka ku boma kuti likhale litakweza pa ntchito anthu onse omwe agwira ntchito mboma kwa zaka zoposera zisanu ndi chimodzi (6). Iye wati kusachitapo kanthu kwa boma pa nkhaniyi kukusonyeza chibwana chachikulu ndipo ati kunyanyala ntchitoku kuchitika mpaka pa 12 June pomwe adzabwerenso ndi ganizo lina ngati boma silichitapobe kanthu. Tikungofuna kulikumbutsa boma kuti lipange zomwe tinalipempha kuti likweze ma a Civil Servants onse omwe akhala pa malo omwewomwewo kwa zaka 6 kupita mtsogolo, anatero a Njolomole. Iwo ati kwa omwe padakali pano sakugwira ntchito apitirize kukhala mmene akukhalira koma kwa omwe amapita ku ntchito atha kumapitabe koma ati asamakakhalitseko monga momwe amachitira kale. ",14 " Afuna chitukuko chofanana mmadera a aphungu Ntchito za chitukuko mmadera oyimiriridwa ndi aphungu a ku Nyumba ya Malamulo chiyamba kufanana tsopano ntchito yodulanso malire ikachitika. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Bungwe loyanganira zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) lati ntchitoyi tsopano ikungodikira katswiri wochokera kunja yemwe adzaigwire. Zonse zatheka tsopano tikungodikira katswiri yemwe achokere kunja kudzagwira ntchito yodulanso malirewa. Katswiriyu sitikumudziwa koma atumizidwa ndi akuluakulu a bungwe la Commonwealth, chidatero chikalata chomwe bungweli lidatulutsa. Mneneri wa bungwe la sisankho mdziko muno, Sangwani Mwafulirwa, adati kudulanso malirewa kuthandiza kuti aphungu onse 193 azikhala ndi madera ofanana komanso chiwerengero chofanana cha anthu. Madera ena pakalipano ndi aakulu kwambiri pomwe ena ndi aangono kwambiri ndiye poti aphungu amagwira ntchito imodzi, tikufuna kuti madera awo akhale ofanana kuti ntchito ikhalenso chimodzimodzi, adatero Mwafulirwa. Iye adati mwachitsanzo dera la chigawo cha pakati mboma la Lilongwe ndicho chili chachikulu kwambiri ndi anthu oponya voti 126 115 pomwe dera la chilumba cha Likoma ndicho chochepetsetsa ndi anthu ovota 6 933 basi. Ngakhale pali kusiyana kotereku ndalama za chitukuko zomwe aphungu amalandira zotukulira madera awo zimakhala chimodzimodzi kutanthauza kuti ndalama zomwezo kwina zikuthandiza anthu ochuluka kuposa kwina. Ngakhale zinthu zili choncho, palinso nkhani yosintha ndondomeko ya kayendetsedwe ka chisankho yomwe kauniuni wa malamulo akale adachitika ndipo komiti yomwe imachita kauniuniyu idatulutsa kale zotsatira zake. Imodzi mwa mfundo zikuluzikulu mndondomeko yatsopanoyi ndi yakuti aphungu asamakhale ndi malire koma kuti boma lililonse lizikhala ndi chiwerengero cha aphungu potengera chiwerengero cha anthu mbomalo. Mwafulirwa adati bungwe la MEC silinganenepo kanthu pa za tsogolo la ntchito yodulanso madera a aphungu potengera malamulo atsopanowa pokhapokha nthambi ya zamalamulo idzanene mfundo yomaliza. Nzoonadi, ndondomeko yatsopanoyi idapangidwa koma sidaperekedwe kunthambi ya zamalamulo (Law Commission). Zonse zidzidziwika nthambiyi ikadzanena maganizo ake. Panopa tiyeni tibatsata zomwe zilipo, adatero Mwafulirwa. ",11 " Anatchezera Ndimufunsirebe? Ndine mnyamata wa mu Lilongwe ndipo ndidagwa mchikondi ndi msungwana wina. Ndakhala ndikuponya mawu kwa iye koma iyeyo amayankha moti savomera kapena kundikana. Kodi ndipitirizebe kumufunsira? Ndithndizeni ndazunzika maganizo. B, Lilongwe. Zikomo B, Ndikuyankha molingana ndi kuti siunandiuze kuti wakhala nthawi yaitali bwanji ukuyesa mwayi wako. Zikuoneka kuti msungwanayo sanapange chiganizo chokulola kapena kukukana. Nthawi zambiri msungwana akakhala mmalingaliro otero nchifukwa chakuti akukukayikira. Chikaikochi chikudza chifukwa pali zina zimene adamva za iwe ndiye akadali kulingalira kuti apange chisankho payekha. Komanso iweyo mwina chidwi chako ukungoonetsa kuti ukumufuna. Tsono akalola, chotsatira chidzakhala chiyani? Mwinatu msungwanayo malingaliro ake ndi akuti akufuna kupeza mwamuna wa banja pamene iwe ukungoonetsa zizindikiro za chibwenzi basi. Pomaliza ndiyenera kukuuza kuti ngati wayesa kumufunsira koma siukulandira yankho loyenera, bwanji osayamba wakhala mnzake nkumacheza zina ndi zina? Akuyenera kukumvetsetsa kaye kuti umaganiza chiyani, nanga umafuna chiyani asanakulole. Izo ndiye udziwe. Mbali inayi, ungodziwanso kuti fupa lokakamoza limaswa mphika choncho ngati watha nthawi yaitali ukuyendera, ndi bwino kuyangana kwina. Nthawi siyibwerera. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Wokwatira wandipatsa mimba Zikomo Gogo, Ndinapanga chibwenzi ndi mwamuna wina amene ankaonetsa Chikondi kwambiri pa ine. Izi zili choncho, mwamunayo sanandiuze kuti ndiwokwatuira koma nditamva kwa ena ndidamufunsa adayankha kuti akufuna kumusiya ndipo andikwatira ineyo. Inetu ndili pasukulu ndipo zisanatheke zoti andikwatirezo, wandipatsa mimba pano akuti ndizikhala kwathu ndipo azingondithandiza. Kodi ndipange bwanji pamenepa. VD, Chiradzulu. VD, Ndi ambiri asungwana ndi amayi amene ali ndi nkhani zotere. Zagwa zatha, ukuyenera kuyangana kutsogolo. Pali zinthu ziwiri zimene ndingakulangize. Choyamba, udziwe kuti ngati wakupatsa mimba, nkhaniyi ukuyenera kuitengera kukhoti la majisitileti. Malamulo atsopano a ukwati akusonyezeratu kuti wopereka mimba nkuthawa akuyenera kubweretsedwa pamaso pa oweruza. Kukhotiko nkomwe akatambasule kuti akuyenera kukuthandiza motani. Chachiwiri chimene ndinganena nchakuti usataye mtima kulekeza sukulu panjira chifukwa uli ndi pathupi. Osataya pathupipo monga ena angaganizire. Ukuyenera kukabereka ndipo ukalera ndi kuyamwitsa mwana wakoyo mwakathithi, udzabwerere kusukulu. Sukulu ndi tsogolo lako lowala ndipo udziwe kuti udzatha kuthandiza bwino mwana wakoyo moti bamboyo adzachita manyazi. Koma osaiwala kutengera nkhaniyi kukhoti. Andipatse mimba? Agogo, Ndinali ndi chibwenzi chimene ndakhala nacho zaka 4 ndipo takhala tikugwirizana za ukwati. Koma posakhalitsapa anangosintha nkumanena kuti akufuna andipatse mimba koma adzandikwatira zaka ziwiri zikubwerazi. Kodi pamenepo pali chikondi? Chonde ndithandizeni. RC, Mzuzu. RC, Apa palibepo chikondi. Akupatse mimba ya chiyani? Adzakukwatira zaka ziwiri zikatha chifukwa chiyani? Zaka 4 zonse zapitazo asanakukwatire akufuna chiyani? Udabwe nazo. Kodi anatu amayenera kukhala mphatso ya mbanja ngakhale ena angathe kukhala ndi chisankho chokhala ndi ana a mwamuna kapena mkazi amene sanakwatirane naye. Choti udziwe, amuna ena amangofuna kukupusitsa. Uyu akhoza kukhala mmodzi mwa amuna otere. Nanga mpaka kukuuza kuti akufuna kukupatsa mimba? Nkutheka iyeyo akuuzanso akazi ena atatu chimodzimodzi. Tsono udzatani nonse mukalolera kutenga mimba kuchoka kwa iye? Khala pansi, sunthapo phanzi asakutaire nthawi. ",12 "Mpoya Akhazikitsa Thumba la Ndalama Zolipilira Ana Sukulu Phungu wa m`dera la Mtonya m`boma la zomba a Nedson Mpoya wati komiti yomwe isankhidwe kuti iyendetse thumba ia ndalama zolipilira ana osowa sukulu fizi m`sukulu Bursary m`derali iwonetsetse kuti yalemba ana oyenera. A Mpoya omwe amayimira chipani cha UDF m`delaro wati ndalama zimenezi ndi Constituency Development Fund (CDF) choncho oyang`anira thummali ndi phungu waku nyumba ya malamulo choncho anthu-wa akuyenera kuonetsetsa kuti pasankhale kukondera kapena katangale posankha ana ovutikawa omwe azilipilipiridwa sukulu ndi komitiyi. Mwazina iye wachenjezanso anthu omwe akumagulitsa ma form ogwilitsira ntchito yolembera ophunzirawa kuti akkapezeka alandila chilango popeza ma form-wa ndi aulele. Chomwe ndikufuna kutanthauza kwambiri tidagozindikira ma form atabwera ku ma constituency kwanthu kuno ndiye timafusa kuti maform-wa abwera bwanji, anatero a Mpoya. A Mpoya ati ndondomekoyi si momwe adakonzera poyamba koma ati zakhala chomwechi chifukwa choti zinthuzi zangochitika mwadzidzidzi. ",3 " Milandu yachepa ku Blantyre Milandu yosiyanasiyana mu mzindawa Blantyre yatsika kuchoka pa 328 mu February chaka chatha kufika pa 204 mwezi omwewo chaka chino, atero apolisi. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Wachiwiri kwa mneneri wa polisi mu mzindawo, Dorrah Chathyoka adati iyi ndi nkhani yosangalatsa. Kutanthauza kuti milandu yomwe anthu amapalamula yatsika ndi 37.8 pa 100 iliyonse. Iyi ndi nkhani yabwino kutsimikizira ntchito yomwe apolisi a Blantyre akugwira usiku ndi usana, adatero Chathyoka. Iye adati polisi yawo idakhazikitsa ndondomeko zothana ndiupandu zomwe zayamba kubala zipatso. Mwazina ndikuyendayenda komwe apolisi akuchita mmadera onse. Ena akumavala zovala za polisi ndi ena zovala zawamba kuti tithane ndi upandu, adatero iye. Izitu zikumachitika usiku ndi usana pamene tikumayenda pa galimoto, njinga komanso ena kuyenda wapansi. Takhazikitsanso zipata mmisewu, tikumatola onse amene akuyenda nthawi yosaloledwa popanda chifukwa chenicheni, adaonjeza Chathyoka. Iye adati zinanso zomwe achita ndikupanga ubale wabwino pakati pa apolisi ndi anthu okhala mumzinda wa Blantyre. Tidakhazikitsa polisi yammadera, tikulankhulana bwino ndi anthu. Komanso kugawana maganizo ngati pafunika kutero. Chathyoka adati kudzera mnjira zotere, apolisi akumanjata owaganizira kupalamula mlandu mosavuta pamene anthu akumawatsina khutu. Anthu akupemphedwa kuti apitirize kupanga ubale wabwino ndi a polisiwa kuti nkhani yabwinoyi ichitika kwa nthawi yotalikirapo. Cholinga ndi kupanga Blantyre wokomera aliyense, adatero. ",7 "Bungwe La Amayi Ku Mphakati Wa St. Clara Lalimbikitsa Amayi Kuthandiza Radio Maria Bungwe la amayi ku mphakati wa St. Clara omwe uli pansi pa St. Dennis parish mu Arch-Diocese ya Lilongwe, lalimbikitsa amayi kuti adzitenga nawo mbali pothandiza Radio Maria Malawi. Wapampando wa bungweli ku mphakatiwu mayi Idah Nkhoma ndi omwe anena izi lolemba pambuyo pa mkumano omwe mphakatiwu unali nawo pomwenso anapezerako mwayi othandiza wailesiyi pa nthawi ino pomwe wailesiyi ikuchita Mariatona. Iwo anati kuthandiza Radio Maria kumathandiza kuti ntchito za wailesiyi zipite patsogolo. Tinawona kuti tikamakumana ngati azimayi, kakangono kamene tilin ako tikuyenera kuthandiza wailesi yathu yomwe imatidalitsa kuti ikathandizenso anthu ena, anatero mayi Nkhoma. Mmodzi mwa amayi omwe anachita nawo mkumanowu mayi Patricia Mwapasa anati ndi okondwa popeza athandiza wailesiyi mu nyengo ino ya Coronavirus pomwe ntchito zambiri zikuoneka kuti zakhudzidwa kwambiri ndipo sizikuyenda bwino. ",13 " Abusa ku HIH ndi zina Tsikulo ndidali pa Wenela kuitanira minibasi monga mwanthawi zonse. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Ndirande iyi! Machinjiri iyo! A Lilongwe achamba atatu iyo yopita! Ndati achangu atatu a Lilongwe iyi! Mukudziwa kale. Nthawi imeneyo nkuti ndikumveratu nyimbo zatsopano zokhazokha, ma headphone ali kukhutu. Pamaphulikatu nyimbo zongomasula kumene: Namadingo adabwera ndi Msati Mseke, Wambali amvekere Asungwana a kwa Chitedze, anyamata a ku Chileka akuti Mr Bossman ndipo Lucius akuti Walema. Osaiwala munthu wamkulu Nkasa akufwamphula Anenere. Ndidachotsa ma headphone mkulu wina atandikodola. Iyetu adali atangotsika basi ndipo ndidadziwiratu kuti ndi mbusa. Musandifunse kuti ndidadziwa bwanji chifukwa sindikuyankhani. Ndipo nkakuuzani kuti ndidaonera mwinjiro wake wakuda, ndi kolala yoyera muchitapo chiyani? Nanga nkakuuzaninso kuti simukudziwa kolala yoyerayi idabwera bwanji mulephera kuyankha. Ndangokhala muno muliyenda kuchoka kwathu kwa Kanduku komwe ndidasiya mkazi wanga wokondeka, Nambe, koma ndimadziwa kuti nthawi imeneyo abusa ankaphedwa pochekedwa makosi. Iyitu idali nthawi yowawitsa pamene kukhala mbusa chidali chinthu choopsa zedi. Komatu abusa anthawiyo adali olimba mtima ndipo adayamba kuika kolala yoyera pakhosi kuti langa ndi limeneli liduleni koma sindisiya kufalitsa uthenga wabwino, kuthandiza kuti ochimwa asinthe ndipo iwo ali olungama apitirize kutero. Ameni? Atsogoleri, inetu wanga ndi wa ku HIH, ndikwere ya chiyani? adandifunsa. Ya Ndirande, kapena ya Machinjiri. Kwerani iyi abusa. Ya Machinjiri ndi K200, ya Ndirande K100. Simufuna bodyguard? Ndikumvatu kwaterera, ndidatero. Adangoseka, uku akukwera minibasi ya Ndirande. Akukwera, ndidaona chisenga chikusuzumira. Madzulo a tsikulo, tili malo aja timakonda pa Wenela, adatulukira Abiti Patuma ali wefuwefu. Mkulu wina wandilipirira kuti ndipeze chitupa choyendetsera galimoto. Koma eeeh! Abale ku Ginnery Corner uku kuli gahena ndithu. Kudikira tsiku lonse uli chiimirire koma chitupa osatuluka, adalira. Bwanjinso nanga? ndidafunsa. Kuli mazunzo. Ena akundiuza ayendera masiku 8 nkhani yomweyi. Ukapolotu uwu. Tsono nthawi yotakata mtaunimu ikhalapo? Ndalama zopereka ndiye simasewera. Akatolera ndalamazo ndiye basi kususa kukhalepo. Osololawo aiwala kuti lero Adona Hilida athawa pano pa Wenela kuopa kukwizingidwa poti ena akuti akukhudzidwa ndi kusolola mopanda manyazi kudagundika ku Kapitolo, adatero Abiti Patuma. Palibe icho ndidatolapo. Mwati chiyani? adafunsa wapamalopo, Gervazzio. Kodi simunamve kuti Mani Rich alembera akatalangwe ena kuti Adona Hilida akusautsidwa mmaganizo ndi anthu amene akusaka moyo wawo? Nanga simunamvenso kuti uja wa mabasi Leo wachita muja adachitira Pitapo, kunena kuti Adona Hilida ndiwo adawatuma kusolola khobidi? adayankha Abiti Patuma. Tonse tidangoti kukamwa yasaa! Man Rich amafatsa! Atatsegula wailesi Gervazzio, tidangomva mkulu uja adawerenga kwambiri vesi yaifupi mbaibulo akulankhula. Mwamuiwala kale mkuluyu? Nanga ndichite kukuuzani za vesi ija imati Yesu analira? Kapena mwamuiwala mkulu woyanganira maula adalira pomwe adanena kuti Moya Pete ndi Dizilo Petulo Palibe ndiwo akadaulo pobera maula? Amene apambana ndi Dizilo Petulo Palibe, Ukafuna Dilu Fatsa komanso Male Chauvinist Pigs, adatero mkuluyo. Posakhalitsa adatulukira Kenny Foot Soldier Nsongo. Atiberanso maula. Panalibe chilungamo pamaula amenewa. Pali kukondera, adali kutero. Shhhhh! Tikumvera nkhani. Mipingo ina idzatha ngati makatani, adatero Abiti Patuma. ",13 " Akufuna fisi alangidwe koopsa Magulu omwe amalimbikitsa maufulu a amayi ati mpofunika mkulu woimira boma pa milandu Director of Public Prosecutions (DPP) Mary Kachale atengere nkhani ya Eric Aniva kubwalo lalikulu. Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Aniva, yemwe adanjatidwa zaka ziwiri kukagwira ntchito ya kalavulagaga kundende atapezeka wolakwa pamlandu wotenga mbali pa miyambo yoopsa pokhala fisi wochotsa fumbi ndi kulowa kufa mboma la Nsanje. Adampatsa zaka ziwiri: Aniva Nkhani ya Aniva idagwedeza dziko atabwera poyera nkuulula kuti wakhala akugwira ntchito ya ufisi kwa nthawi yaitali ndipo adagonana ndi amayi ndi atsikana oposa 100. Koma magulu a amayi, motsogozedwa ndi mabungwe a Malawi Human Rights Resource Centre (MHRRC), NGO Gender Co-ordination Network (NGO-GCN) ndi African Womens Development and Communications Network (Femnet), ati chigamulo chomwe Aniva adalandira lachiwiri lapitali nchochepa. Maguluwa ati potengera mlandu wa Aniva, ufulu wa amayi sudalemekezedwe kotero amayenera kulandira chilango chokhwima osati zaka ziwiri basi. Ndife okhudzidwa kuti munthu yemwe ali ndi kachilombo ka HIV komwe kamayambitsa matenda a Edzi ndipo amapitiriza kugona ndi amayi ndi ana achichepere mpaka zaka 12 angalandire chilango chochepa chonchi. Ndi uthenga wanji omwe tikupereka kwa abambo ena akhalidwe longa lomweli? Zaka ziwiri basi mlandu wonsewu? Uku nkunyoza amayi ndipo bwalo la milandu likuyenera kuunikapo bwino nkusintha chigamulochi, adatero mkulu wa bungwe la MHRRC Emma Kaliya. Mabungwewa adati ngati nkhani yoyamba ya mtunduwu yoweruzidwa pogwiritsa ntchito lamulo latsopano la za ufulu wa anthu, Aniva amayenera kulandira chilango choletsa khalidweli. Naye mkulu wa zophunzitsa anthu kubungwe la Femnet, Hellen Apila, adati apa dziko la Malawi waphonya mwayi waukulu wopera chenjezo kwa anthu omwe salemekeza ufulu wa amayi potsatila miyambo. Bwalo la Magistrate ku Blantyre lidagamula Aniva lachiwiri lapitali kuti akagwire ntchito yakalavulagaga kundende atavomera kuti amachita mwambo wa fisi akudziwa kuti ali ndi kachilombo ka HIV. ",7 "Papa Wati Ali Limodzi Mmapemphero ndi Mzika za ku America Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco watsimikizira a Katolika ndi anthu onse ku United States of America kuti ali nawo limodzi mmapemphero. Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican, Papa walankhula izi lachinayi kudzera mu uthenga wake wa pa lamya kwa President wa bungwe la ma episkopi a mpingo wa katolika mdziko la America, Archbishop Jose Gomez wa archdiocese ya Los Angeles. Iye wayamikira maepiskopi a mpingo wa katolika mdziko la United States of America chifukwa chosonyeza utsogoleri wabwino pomwe mdzikolo mukuchitika ziwawa chifukwa cha imfa ya nzika ya dzikolo, George Floyd. Kudzera mu uthenga wa pa lamya-wo Papa Francisco wati ali pafupi ndi anthu mdzikolo pa nthawiyi ndipo akuwapempherera. Papayu wayamikiranso maepiskopi a Mpingo wa Katolika podzudzula mchitidwe wa tsankho mdzikolo womwe wachititsa kuti George Floyd aphedwe. Papa Francisco wauza Archbishop Gomez pa lamyayo kuti mwapadera waikiza mmapemphero Archbishop Bernard Hebda ndi Mpingo wonse ku Minneapolis mdzikolo komwe Floyd adaphedwera. Lachitatu pa 3 June 2020 Papa Francisco adadzudzula kuphedwa kwa nzika ya chikudayi mdzikolo. George Floyd adaphedwa ndi wapolisi wina pa 25 May, 2020 ndipo padakali pano anthu ena asanu aphedwanso pa zionetsero ndi zipolowe zomwe anthu akuchita powonetsa kusakondwa kwawo. ",13 "Boma Lilonjeza Kumanga Ubale ndi Mpinga wa Katolika Wolemba: Thokozani Chapola Boma lati liyesetsa kumanga ubale wabwino ndi mpingo wakatolika mdziko muno. A Ralph Jooma omwe ndi nduna ya za mtengatenga ndi zomangamanga, kudzanso a Bright Msaka omwe ndi nduna ya zamalamulo anena izi pa mwambo wokhadzikitsa chimbale cha nyimbo zomvera ndi kuonera za kwaya ya mpingo-wu ya St. Annie ku St. Louis Montfort Parish ku Balaka mu dayosizi ya Mangochi. Iwo ati boma limadziwa zakufunika komanga ubale wabwino ndi mpingowu. Polankhulanso mmodzi mwa aphungu a chizimayi mboma la Balaka, mayi Bertha Mackenzie Ndebele anayamikira ntchito yotamandika yomwe mamembala a kwayi akugwira pofalitsa uthenga wabwino kudzera mu mayimbidwe. Kumwambowu kunafikanso a ndale ena monga olemekezeka a Chifundo Makande MP, kudzanso a Shadrick Namalomba MP. Mutu wa chimbale cha nyimbo zomvera ndi kuonera zomwe kwayayi yakhazikitsa ndi Ndanyamuka. ",14 "Dziko la DRC Latulutsa Akayidi 1200 Kaamba ka Coronavirus Unduna wa zachilungamo mdziko la Democratic Republic of Congo, watulutsa akayidi okwana 1,200 pofuna kuchepetsa kuchulukana kwa akayidi mndendezi ngati mbali imodzi yolimbana ndi kufala kwa kachilombo ka Coronavirus. Malingana ndi nduna mu undunawu Celestine Tunda, ena mwa omwe amasulidwa ndi omwe anali ndi milandu ingoingono. Ndende ya Makala yomwe ili mu mzinda wa Kinshasa ndi imodzi mwa ndendezi ndipo yamasula akayidi okwana 700. Ndunayi yati akayidi enanso akhala akumasulidwa posachedwapa ndipo yapempha oweruza milandu kuti azimanga okhawo omwe apalamula milandu ikuluikulu monga ya kupha ndi yogwirira. Mdziko la Democratic Republic of Congo mwapezeka anthu okwana 180 omwe ali ndi matendawa ndipo ena 18 amwalira. Padakalipano boma la dzikolo layimitsa zochitika zonse za mdera la Gombe mu mzinda wa Kinshasa kwa sabata ziwiri kaamba ka vutoli. ",6 " Bullets, manoma akunthana lero Kumakhala fumbi nthawi zonse Bullets (zifiira) ndi Wanderers akamakumana Tsoka mtunda ndi nyanja popeza woipayo watsikira pa Civo Stadium masanawa. Ligi ya TNM Super League tsopano yafika pa gwiritse. Nkhawa ili biii! Kwa osapotera timu ya Big Bullets ndi Mighty Wanderers pamene matimuwa akhale akuphananso masanawa. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Iyi ikhala nkhondo yeniyeni chifukwa ngati Nyerere zipambane masewero asanu amene yatsala nawo ndiye kuti zikhala ndi mapointsi 55 kutanthauza kuti iposa matimu onse. Apa ndiye kuti zili ndi mwayi wophulanso ligiyi patangodutsa mwezi zitanyamula chikho cha Standard Bank. Koma mwina loto la Wanderers lingakhale lovuta chifukwa mphunzitsi watsopano wa Bullets, Gerald Phiri, akuti akulotanso atapambana masewero asanu amene timuyi yatsala nawo kuti mwina angathere pabwino kapena kutenga ligi. Bullets ikuchokera kolepherana mphamvu ndi Blantyre United. Iyo ili pa nambala 6 ndi mapointsi 36. Pamene Nyerere zikuchokera koboola jombo ya Moyale ku Balaka ndi zigoli ziwiri kwa duuu! Izo zili pa nambala yachiwiri ndi mapointsi 40 kutsogozedwa ndi Red Lions yomwe ili ndi mapointsi 41 koma yatsala ndi magemu anayi. Masewero a Wanderers ndi Bullets ali pa Civo pamene pakhale pakhomo pa Nyerere. Timuyi ndiyo yasankha bwaloli chifukwa pa Kamuzu idathamangitsidwa patachitika ziwawa ndipo siidamalize chilango. Koma mlembi wa Nyerere David Kanyenda akukhulupirira kuti lero Maule aona mbonaona. Mukaonetsetsa takhala tikuchita bwino, sitikuchinyitsa zigoli. Tikuchokera kopambana ndi Moyale, ndipo dziwani kuti Bullets ndi akazi athu, akutero Kanyenda. Matimuwa akumanapo kawiri posakhalitsapa. Mndime yoyamba ya ligiyi, matimuwa adalepherana mphamvu pochinyana chigoli chimodzi kwa chimodzi. Matimuwa adakumananso ku Lilongwe mubonanza ya Luso TV pomwe Bullets idapambana kudzera mmapenote. Matimu ena akhalenso akuphana mchikhochi masanawa. Mzuzu United ikhomana ndi Civo United pa Mzuzu Stadium. Evirom ithyolana ndi Blue Eagles pa Kamuzu. Jombo ya Red Lions ili pakhomo ndi Kamuzu Barracks ku Zomba. Mawa, Blantyre United iphwanyana ndi Blue Eagles pa Kalulu Stadium. Epac F.C ikwapulana ndi Silver Strikers pa Civo Stadium. Moyale ikumana ndi Civo United pa Mzuzu Stadium. Azam Tigers igogodana ndi Kamuzu Barracks ku Balaka Stadium. Evirom ikumananso ndi Mafco FC pa Kamuzu Stadium. ",16 "DPP, UDF Asayinira Mgwirizano Zipani za United Democratic Front (UDF) ndi Democratic Progressive (DPP) zati ndi zokonzeka kugwilira ntchito limodzi potukula dziko la Malawi. Muluzi (kumanzere) ndi Mutharika kusonyeza mgwirizano wawo Zipanizi zanena izi lachiwiri kunyumba yachifumu ku Lilongwe pomwe zimasayinirana mgwirizano kuti zigwilira ntchito limodzi pamene akukonzekera chisankho cha Pulezident chomwe chichitike pa 19 May chaka chino. Atsogoleri a zipani ziwirizi a Peter Mutharika komanso a Atupele Muluzi ati ndi okonzeka kugwilira ntchito limodzi kamba koti zipani zawo zimatsatira mfundo zofanana. Amayi a DPP komanso UDF kuvinira limodzi Pa 3 February chaka chino bwalo la milandu ya zamalamulo linalamula kuti chisankho chomwe chinachitika mdziko muno pa 21 May chaka chatha ndi chosavomerezeka ndipo chichitikenso pasanathe masiku 150 kuchokera patsikuli. Ndipo kutsatira izi nyumba ya malamulo yagwirizana kuti chisankhochi chichitike pa 19 May 2020. ",11 " Atudzula ziwalo za mwamuna wake Pamene nkhanza zambiri zomwe zimachita zimakhakla zochokera kwa abambo kupita kwa amayi, Loveness Nakayuni wa mmudzi mwa Chapyoka, T/A Mwaulambia mboma la Chitipa, masiku apitawa adali mchitolokosi pomuganizira kuti adafinya mwamuna wake kumalo obisika mpaka kutudzula ziwalo. Mneneri wa polisi mchigawo cha kumpoto Maurice Chapola adatsimikiza za nkhaniyi pouza Msangulutso kuti mayiyo adali mmanja mwawo kaamba kovulaza mwamuna wake, Winis Kita, wa zaka 46, atamugwira kumoyo chifukwa akuti adaphwanya lonjezo logona kunyumba kwake. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Iye adati Kita, yemwe ndi wamitala, adanyamuka kupita kukamwa mowa komwe adabwerako madzulo. Iye adafikira kunyumba kwa mkazi wake woyamba, Nakayuni, koma sadakhalitse ndipo adapita kunyumba ya mkazi wake wamngono. Izi zidamuwawa Nakayuni, yemwe adamulondola mwamunayo kunyumba kwa mkazi wake wamngonoyo. Atafika adapeza mwamunayo atakhala pakhonde akusuta fodya. Nakayuni adangombwandira malo obisika a mwamuna wakeyo nkufinya mpaka kutudzula, adafotokoza Chapola. Iye adati Kita adamutengera kuchipatala cha boma komwe adalandira thandizo lobwezeretsa ziwalozo zake mchimake. Pano akuti akupezako bwino ndipo akuchita kuyendera kukalandira mankhwala kuchipatala. Funso nkumati kodi banja lilipobe apa? Tidalephera kuyankhula ndi Kita, koma wapolisi wa zofufuzafufuza, teketivu Yatamu Kasambara, adauza Msangulutso kuti mkuluyu adakatseketsa mlandu kupolisiko ponena kuti zidali zambanja ndipo mkazi wake pano ali kunyumba ati azikalera ana. Ku Chitipa komweko, mayi wina, Mawazo Nzunga, akumuganizira kuti wapha mlamu wake atamumenya ndi mpini wa khasu pamutu atalephera kumvetsetsana pankhani ya chakudya. Chapola adauza Msangulutso kuti wophedwayo, Willard Mwilenga, adapita komwa mowa ndipo pochoka kumowako adaganiza zokapempha chakudya kunyumba ya mbale wake komwe adauzidwa kuti chakudya chake kulibe. Yankho la mlamu wakeyo silidamusangalatse ndipo kaamba ka kuledzera adayamba kummenya. Nzunga pobwezera adatenga mpini wa khasu ndipo adamugogoda nawo pamutu nkumukomola nawo, adafotokoza Chapola. Mwilenga adathamangira naye kuchitapatala cha Kameme koma ataona kuti zawakulira adamutumiza kuchipatala chachikulu ku Chitipa komwe adakafera. Chapola adati Nzunga ali pa rimandi pandende ya Chitipa kudikira kuyankha mlandu wa kupha munthu. Pothirapo ndemanga pankhani za nkhanza, wapampando wa bungwe la NGO Gender Coordination Network, Emma Kaliya, wati nkhani kuti itengedwe kuti ndi ya nkhaza kwa amayi kapena abambo zimakhala bwino kuyangana chatsitsa dzaye kuti njovu ithyoke mnyanga. Mboma la Chitipa amuna ndi azikazi awo ali ndi kachisimo kokamwa mowa ku chilabu limodzi, makamaka madera a kwa Kameme ndi Mwaulambia. Tikuyesetsa kuthana ndi mchitidwe womwa mowa ku chilabu chifukwa tikukhulupirira kuti umakolezera nkhaza pakati pa amayi ndi abambo, adatero Kaliya. ",15 " Ndidamuona koyamba mu Shoprite Kwangotsala mwezi umodzi kuti anthu adzathyole dansi paphwando la ukwati wa Evance Mwale ndi Tiwonge Nundwe pa 4 May. Evance amagwira ntchito ku Sinodi ya CCAP ya Livingstonia pomwe bwenzi lakelo ndi muulutsi pa wailesi ya Voice of Livingstonia. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Awiriwa akhala pa ubwenzi kwa zaka zitatu. Malinga ndi Mwale, adamuona koyamba Nundwe mu Shoprite ku Mzuzu, ndipo adamusangalatsa. Tidakumana koyamba mchaka cha 2015 mu Shoprite ndipo adandipatsa chidwi mpaka ndidayamba kumufufuza ndithu kuti ndimudziwe bwino lomwe monga kwawo komanso kudziwa zomwe amachita, adalongosola Mwale. Ndipo iye adati anthu akufuna kwabwino adamuuza zonse za namwaliyu. Komatu Mwale adali ndi mwayi chifukwa mchaka chomwecho adapeza danga lokagwira ntchito kuofesi ya Nundwe komwe sadachitenso za bo! bo!bo! koma kuyamba kucheza ndi mtsikanayo. Ndipo pofika chaka cha 2016, ubwenzi wa ponda-apa-nane-ndipondepo udayambika pakati pa awiriwa. Ndidamufunsira ndine chifukwa adalibe nane chidwi olo pangono kuti nkukhala nane paubwenzi wokathera mbanja. Zidanditengera miyezi isanu ndi umodzi kuti andipatse danga lokhala naye pa ubwenzi, adalongosola Mwale. Komatu monga zikhalira, ubwenzi uliwonse umakhala ndi zokhoma zake ndipo nawo awiriwa akumana nazo zokhoma zofuna kuwalekanitsa, koma Chauta waikapo dzanja kuti amange banja. Pomwe Mwale adamutsira diso Nundwe koyamba mu Shoprite, namwaliyo adamuona koyamba Mwale pomwe adakayamba kuphunzira ntchito kusinodiyi. Kumayambiliro timacheza monga munthu ndi mnzake, koma sindidaganizeko zoti awirife nkukhala paubwenzi, koma ndi nthawi, tidayamba kucheza kwambiri mpaka anthu kumaona ngati tili paubwenzi pa nthawiyo, pomwe sizidali chomwechi, adalongosola Nundwe. Iye adati chikondi cha awiriwa chidayambira pomwe ankapitira limodzi kokadya nkhomaliro mmalo odyera mumzinda wa Mzuzu. ",15 " Kukokana pa za amayi ovina Jameson: Mzimayi abise thupi Zusamvana komwe kudabuka pa zakayendetsedwe ka bungwe la Asilamu la Muslim Association of Malawi (MAM) kwayamba kufalikira mmaboma ambiri tsopano. Magulu a anthu osiyanasiyana omwe akumadzitcha kuti ndi Asilamu okhudzidwa ayamba kulankhulapo pankhani yofuna kuchotsa wapampando wa bungweli, Idrisa Muhammad, yemwe akuti akuphwanya ngodya za chiphunzitso cha chipembedzochi. Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Koma Muhammad watsutsa za nkhaniyi ndipo wati sakugwedezeka chifukwa palibe munthu kapena bungwe lomwe lingamuchotse pampandowo. Iye wati akuganiza kuti magulu omwe akuchita izi akutumidwa ndi akuluakulu ena mchipembedzochi omwe sakumufunira zabwino ndipo walonjeza kuti sagonjera anthu oterewa. Ndikudziwa kuti alipo ena ake omwe akuwatuma kuti azichita zimenezi koma saphulapo kanthu chifukwa ngakhale atachita bwanji palibe yemwe ali ndi mphamvu zondichotsa pampando komanso sindingalole kutula pansi udindo wotsogolera chipembedzochi, watero Muhammad. Magulu omwe akulimbikitsa kuti Muhammad atule pansi udindo wake akuti mkuluyu walephera kugwiritsa chiphunzitso cha Chisilamu polola amayi achipembedzochi kuvina pamisonkhano ya ndale ndi kugwiritsa ntchito nyimbo za Chisilamu zimene angozisintha potamanda andale. Limodzi mwa magulu omwe sakukondwa ndi mtsogoleriyu ndi bungwe loona kuti zinthu mChisilamu zikuyenda mwachilungamo la Muslim Commission on Social Justice. Mtsogoleri wa bungweli Abdul-Aziz Shouaib Jameson wati amayi a Chisilamu saloledwa kulankhula kapena kuvina pamalo omwe pali abambo. Jameson wati amayiwa ndi ololedwa kutenga nawo mbali pandale, koma osati kudzera mchipembedzo. Chiphunzitso chathu chimanena kuti mzimayi abise thupi lake komanso asalankhule pomwe pali abambo pokhapokha ngati ali awiri ndi mwamuna wake, watero Jameson. Kuyambira pomwe nkhaniyi idaphulika sabata zitatu zapitazo mumzinda wa Blantyre pomwe gulu lina limafuna kukatseka ofesi ya Muhammad, gulu lina lidachititsa msonkhano wa atolankhani mumzinda wa Lilongwe pankhani yomweyi. Lachisanu lapita gulu lina mboma la Salima lidachita zionetsero zoti sakusagwirizana ndi wapampando wa bungweli ndipo lidakapereka kalata kwa bwanamkubwa wa bomalo chosonyeza kusakondwa ndo mtsogoleriyo. ",11 "Papa Wati Akhristu Aphunzire Kukonda Anzawo Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wadzudzula khalidwe lodzikonda pakati pa anthu. Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican, Papa walankhula izi lachiwiri pomwe amakumana ndi ana omwe akuchita masewero osiyanasiyana komanso mapemphero ku likulu la mpingowu ku Vatican. Iye wauza anawa kuti moyo umakoma ngati munthu ali ndi abwenzi ndipo ndi kofunika kuti iwo akhazikitse ma ubwenzi abwino ndi anzawo Atatha kulankhula kwa anawa, Papayu anachezanso ndi omwe akuyanganira anawa komanso kuthandizira pa zina ndi zina asanabwerere kunyumba yake yomwe amakhala ya Casa Santa Marta kapena kuti Nyumba ya Marita Woyera. Zochitikachitika za anawa zinayamba kumayambiriro a mwezi uno ndipo pali masewero osiyana-siyana, kuphunzira zina nzina komanso kuchita mapemphero. Ena mwa masewero omwe akuchitika ndi masewero a mpira wa miyendo (football), tennis, basketball, kusambira (swimming) pongotchula ochepa. Zonse zikuchitika motsata ndondomeko zoyikika pofuna kupewa nthenda ya Covid 19. Anawa omwe alipo pafupi 100 ndipo a zaka zoyambira zisanu (5) mpaka zaka khumi ndi zinayi (14) ndi ana a anthu omwe amagwira ntchito zosiyana-siyana ku Vatican. ",14 "Awanjata Kaamba Kobera Agent wa Mpamba Apolisi mboma la Chikwawa amanga amuna awiri kaamba kowaganizira kuti apalamula mualandu wakuba ndalama mu phone kudzera mu njira ya mpamba. Malinga ndi wachiwiri kwa wofalitsa nkhani mbomalo Sergeant Dickson Matemba amunawa ndi Yamikani Mukhoya wazaka 29 komanso James Mbewe wazaka 21 zakubadwa.