Text
stringlengths 292
6.6k
| labels
int64 0
19
|
---|---|
CWO Ilimbikitsa Ukhondo Mu Msika Wa Ndirande Wolemba: Thokozani Chapola Wapampando wa bungwe la amayi a chikatolika mdziko muno Mayi LUCY VOKHIWA lachisanu lapitali walimbikitsa amayi achikatolika mdziko muno za ubwino wodzipereka pa ntchito zosamalira madera awo.
Mayi VOKHIWA ndiwo alankhula izi pa msika waukulu wa NDIRANDE mu mdzinda wa BLANTYRE pamene amayi a mu ARCH DAYOSIZI-yi anatsogolera ntchito yosesa mu msika-wu.
Zomwe tachitazi ndi zomwe tinagwirizana pa msonkhano wathu waukulu wa amayi achikatolika pa dziko lonse umwene timati WUCWO. Nkhani ndi yakuti amayi achikatolika titengepo mbali posamalira madera athu amene tikupezeka, anatero mayi Vokhiwa.
Iwo ati ntchito ya mtunduwu yachitikanso kale mmizinda ya Mzuzu ndi Lilongwe pomwe amayi a mu mzinda wa Mzuzu anakasesa ku chipatala chachikulu cha mzindawo pomwe amayi a mu mzinda wa Lilongwe anakasesa mu msika waukulu wa mu mzindawo.
Polankhulanso wapampando wa komiti yoyendetsa ntchito za pa msika wa Ndirande a CHANCY WIDONI anayamikira amayiwa kamba kosamalira malowa.
Tiwathokoze kwambiri amayi a mpingo wa katolika amene abwera kuzasamalira msika wathu umene unali onyasa kwambiri koma chifukwa cha ntchito yawo msikawu waoneka bwino kwambiri, anatero a Widon.
Iwo apemphanso mabungwe, magulu komanso anthu ena akufuna kwa bwino kuti athandizire pa ntchito za ukhondo mu msikawu omwe ati ndi ovuta kwambiri.
| 6 |
Radio Maria Malawi Celebrates 20th Anniversary in Broadcasting, Evangelisation By Thokozani Chapola Radio Maria Malawi a member of 71 Radio Marias of the World Family in the whole world and 22 countries in Africa was launched on 24th August 1999 in Mangochi by the then bishop of Mangochi diocese of the Catholic church, the late Allessandro Assolari.
Reaching this far the radio organized an event marking its 20th anniversary in the broadcasting industry where evangelization has been its main agenda. The event took place today the 28th of September at the radios premises in the lakeshore district.
In his message, National Coordinator for Radio Maria Malawi, Louis Phiri says that the radio has so far done its part in changing peoples lives spiritually.
Our job has been evangelization and we believe in these 20 years we have done our part in bringing back lost souls to God our Father, he said.
Phiri said that despite several challenges that the radio has been facing like debts that it has been falling into to facilitate its operations, in 20 years the radio has managed to build sub studios in 5 dioceses out of all the 8 dioceses of the Catholic church in the country plus its main broadcasting house in Mangochi diocese.
We do not have studios only in Chikwawa and Karonga dioceses but we have in all the 6 dioceses. We have transmitters everywhere in the country which makes our evangelization reach all people in the country as well as outside the country because we are also streaming live on the internet, said Phiri.
However, Phiri has pleaded with well-wishers to help the station for the success of the 20th Anniversary celebrations.
Radio Maria Malawi uses volunteers as its main human resource for running the airwaves. As one of the longest serving volunteers of the station Emmaunel Kaliati explains, the radio has tried to sharpen the spiritual life of its volunteers.
Personally Radio Maria Malawi has made me to become a mature person and to become a prayerful person because as we are here, we are told prayer comes first, said Kaliati.
In his remarks one of the radios listeners based in Blantyre, Pax Lucius Chimtengo says that the radio throughout its 20 years of evangelization has tried to bring back lost Christians, bring back love in families that were almost dead and it has taught him some things that he wouldnt know.
Without Radio Maria personally I wouldnt know the meaning of miracles. Radio Maria has also mended some families that were on the verge of ending because of its homily. This has also made some Catholics that went out of the church to come back into the church. It has also helped Christians from other churches in bringing them closer to Christ, said Chimtengo.
However, Chimtengo has urged his fellow listeners and all people of good will to continue with helping the radio in cash or kind so that it continues with its job of evangelizing to the masses.
| 13 |
Kudya moyenera nkofunika Kudya ndi moyo koma woona za kadyedwe koyenera ku Lilongwe University of Agriculutre and Natural Resources (Luanar), Dr Alexander Kalimbira, wati munthu amayenera kudya moyenera kuti akhale ndi umoyo wabwino.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Iye adati kudya moyenera ndi gwero la umoyo wangwiro komanso chitukuko cha dziko.
Kalimbira adati ngati munthu akudya moyenera molingana ndi momwe thupi lake likufunira, amakhala ndi moyo wathanzi ndi wosangalala kotero amagwira ntchito molimbika koma ngati akudya mochepekedwa kapena mopyola muyeso, zotsatira zake ndi matenda osiyanasiyana omwenso akutenga kwambiri miyoyo ya anthu.
Pali magulu 6 a zakudya Tikati kudya moyenera sitikutanthauza kuti munthu akuyenera kumadya nsima ndi ndiwo zochuluka ayi koma kudya zakudya zamagulu okwanira pakutha patsiku koma mosadziunjikira. Ngati munthu akudya chakudya chochepa kwambiri komanso chosowekera michere ina, zotsatira zake zimakhala kutupikana, kupinimbira ndi mavuto ena makamaka kwa ana komanso ngati munthu akudya mopyola muyeso, mafuta amachuluka mthupi ndipo mapeto ake ndi matenda osiyanasiyana monga mtima, kudwala nthenda ya shuga, kuthamanga magazi ndi mavuto ena, iye adatero.
Iye adati munthu amayenera kumadya chakudya cha magulu onse 6 pamlingo woyenera chifukwa pali zakudya zina michere yake ikachulukitsa mthupi, imayambitsa mavuto osiyanasiyana. Mwachitsanzo, ngati munthu akuchulutsa kwambiri nsima kapena zakudya zamafuta kwambiri kapenanso za shuga kwambiri, mapeto ake sikelo yake imadzakhala yokwera mopyola muyeso.
Mmalo modya nsima kapena mpunga wochuluka, anthu ayenera kuonjezera tizakudya ta magulu angapo monga kuika pambali masamba, tinyemba, chipatso ndipo pakutha pa zonsezo, munthu umakhala okhuta koma osatenga michere yochuluka yomwe ikhonza kuunjikana mthupi nkuyambitsa mavuto osiyanasiyana, iye adatero.
| 6 |
Mzika za ku Zimbabwe Zipezeka ndi Matumba 66 a Chamba Wolemba: Glory Kondowe 9/08/IMG-20190829-WA0022.jpg 413w" sizes="(max-width: 604px) 100vw, 604px" /> Apolisi mboma la Nkhotakota akusunga mchitokosi mzika ziwiri za mdziko la Zimbabwe kamba kopezeka ndi matumba 66 a chamba zomwe ndizotsutsana ndi malamulo a dziko lino.
Wachiwiri kwa mneneri wa apolisi mboma la Nkhotakota Sergeant Paul Malimwe wati awiriwa omwe ndi a Emmanuel Chisandule a zaka 24 zakubadwa komanso a Forwad Mudekwa a zaka 42 zakubadwa.
Awiriwa ati anamangidwa ndi apolisi-wa loweruka pa 31 August 2019 pamalo ochita malonda a Nkhotakota trading Centre pamene awiriwa amayendera galimoto ya mtundu wa truck pamene amachokera ku dwangwa kubwelera mdziko la kwawo ku Zimbabwe kudzera nsewu wa Nkhotakota-Salima.
Tinanagwira mzika ziwiri za dziko la Zimbabwe omwe ananyamula matumba 66 amankhwala ozunguza bongo zomwe zina chitika mbanda kucha wapa 31 August omwe anagwiritsa nseu wa M5 wa Nkhotakota Salima pambuyo potsinidwa khutu ndi mzika zakufuna kwabwino ndipo tinamanga road block yongoyembekezerapo zomwe zinapangitsa kuti tiwagwire mosavuta, anatero Sergeant Malimwe.
Powonjezerapo a Malimwe apempha a Malawi akufuna kwabwino kuti apitilize kutsina khutu apolisi pankhani zikulu zikulu ngati izi kuti anthuwo azimangidwa ndi kukayankha milandu kubwalo la milandu.
| 14 |
Aletsa zionetsero ku Nkhata Bay Gulu la anthu omwe amakonza zionetsero zofuna kukakamiza boma kuti likonze msewu waukulu wopita ku Mzuzu, limange msika komanso malo oimira basi mboma la Nkhata Bay lidagwetsa ulesi anthu Lachitatu lathali pomwe zionetserozo zidalephereka mwadzidzidzi.
Makomiti atatu a zachitukuko mmadera a ma T/A Timbiri, Mankhambira ndi Mkumbira ataona kuti zitukuko zikuchedwa kukwaniritsidwa mbomalo, adagwirizana zochita chionetsero ndi kukapereka chikalata ku ofesi ya DC wa bomalo.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Gululo lidagwiritsa ntchito gawo 30 la malamulo oyendetsera dziko lino omwe amakamba za ufulu wa anthu pachitukuko.
Koma tsiku la zionetserozi litafika, anthu adauzidwa kuti bwanamkubwa (DC) wa bomali sadapereke chilolezo ndipo ngati anthuwa angapitirire ndi zionetserozi zikhala zosaloledwa.
Kaunda: Ngati sakutiuza zomveka tipitirira ndi zionetsero Ena mwa anthu omwe amafuna kutenga nawo mbali pazionetserozo adadzidzimuka atauzidwa atafika kale pamalo a nkhumano kuti zionetserozo zalephereka.
Nawo apolisi ovala zamawangawanga omwe adalipo 16 sadalekerere koma kuchoka mumzinda wa Mzuzu kukasonkhana nawo pamalo a nkhumanowo pa roadblock yaikulu mbomali. Koma patatha maola awiri opanda chochitika adabwerera ku Mzuzu.
Mneneri wa polisi mchigawo cha kumpoto, Maurice Chapola, adati apolisiwo adangopita kukakhala tcheru posungitsa bata ngati zionetserozo zikadapitirira.
Msangulutso adalankhula ndi wampando wa komiti yomwe imakonza zionetserozi, Mabvuto Kaunda, yemwe adati bwanamkubwa wa bomali ndi amene adaletsa zionetserozi.
Monga mwa malamulo a dziko lino zionetsero zimachitika pokhapokha ngati padutsa masiku awiri mutapereka kalata yanu yodziwitsa DC. Ife tidatsatira izi bwino lomwe chifukwa tidapereka kalata yathu Loweruka sabata yatha kuwadziwitsa kuti tichita zionetsero Lachitatu, adatero Kaunda.
Koma Kaunda adati adali odabwa atauzidwa ndi DC Lachiwiri kuti zionetserozo sizikhalako kaamba koti Lolemba lidali latchutchi choncho sangaliwerengere.
Ifetu zionetsero zathu zikadakhala za bata ndipo timafuna kukapereka kalata kudzera ku ofesi yawo yopita kuofesi ya mtsogoleri wa dziko lino yoti ngati satiyankha zakuspa pamasiku 30, tidzayamba kugona kuofesi ya bwanamkubwayu, adatero Kaunda.
Iye adati anthuwa atopa ndi kulonjezedwa zitukuko zomwe sizikukwaniritsidwa. Kaunda adati ngakhale boma lidayamba kulonjeza zoti likonza msewuwu ndi ndalama zochokera ku bank ya African Development Bank (AfDB) zaka zapitazo, pamalopa palibe ndi kontilakita yemwe.
Tidamvetsedwanso kuti kudaperekedwa K368 miliyoni yomangira depoti ndi msika, koma zonsezi kuli zii, adadandaula Kaunda.
Iye adati bwanamkubwayu wauza komitiyi kuti a unduna wa za mayendedwe komanso bungwe loona za misewu mdziko muno la Roads Authority (RA) akumana nawo kuti athetse kusamvanaku.
Koma ife tikuti, ngati sakatiuza zomveka, tipitirira ndi zionetsero, adatero Kaunda.
DC wa bomali, Alex Mdooko, sadapezeke pa lamya zake zonse ziwiri pomwe timasindikiza nkhaniyi.
Koma mneneri wa bungwe la RA, Portia Kajanga, adavomereza kuti ntchitoyi yachedwadi. Iye adati koma apa nguluwe yalira msampha utaninga chifukwa ati ntchitoyi iyamba posachedwappa.
Ntchito yatha kale, inde tachedwa koma anthuwa asade nkhawa, zitheka osati chifukwa atiopseza koma potsatira dongosolo lake, adatero Kajanga.
Ntchito yomanga msewu idakhazikitsidwa mwezi wa July mchaka cha 2013 ndipo panthawiyo ntchitoyi imati itenga ndalama zokwana K14.8 biliyoni ndipo imayembekezereka kugwiridwa kwa zaka zinayi mpaka chaka cha 2017.
| 11 |
Tidacheza nawo bwanji? Mchaka cha 2015 tamva zikhulupiriro, miyambo komanso mbiri zosiyanasiyana za maderanso osiyana. Lero BOBBY KABANGO akutibweretsera macheza ochepa amene nkhani yake idatekesa anthu.
Afisi ogulitsa ku Dedza Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Nkhani iyi idadzidzimutsa anthu ambiri kumva kuti pali bambo wina amene akugulitsa afisi. Iye adati fisi wamkazi ndiye amadula pamtengo wa K9 000 ati chifukwa akakuswera pamene wamphongo amapanga K8 000.
Mkuluyu ndi Njale Biweyo wa mmudzi mwa Masakaniza kwa T/A Kaphuka mboma la Dedza.
Biweyo adati ntchito ya afisiwo ndi kuteteza usiku, kusakira nyama komanso kukwera ngati muli paulendo. Adati fisi ndi ndege yapansi yomwe imathamanga kwambiri.
Pamene timacheza naye, mkuluyu nkuti ali ndi afisi awiri koma adati ena adawagulitsanso chifukwa adali nawo asanu.
Iye adati adayamba mu 1965 kuweta afisi. Iye ntchito yake akuti ndi ya ulonda ndipo kudzera mtchitoyi, adapeza nawo afisiwa amene amamuthandiza pantchito yake. Komwe kukukhala mkuluyu adatilozera ampingo wina womwenso ukutetezeka ndi fisi wamkazi.
Dzina la Kachindamoto lidabwera bwanji? Chaka chimenechi tidacheza ndi Senior Chief Kachindamoto wa mboma la Dedza amene adatifotokozera momwe dzina lake lidabwerera.
Mfumuyi idati Chidyaonga ankamenya nkhondo kwambiri ndipo sankaopa. Azungu amene ankamenya nawo nkhondoyo adagonja ndi Chidyaonga. Anthu poona momwe mkuluyu akumenyera nkhondo adangomutcha dzina la Chidyaonga.
Mfuti kuti itulutse chipolpolo mukaomba nchifukwa cha wonga umene ukayaka umaphulika kuti phuu! Ndiye chifukwa ankalimbana ndi zimenezi, anthu adangoti Chidyaonga, kutanthauza kuti akumadya wonga wa mfuti.
Kachindamoto nayenso sankaopa nkhondo. Iyeyu sankaopa ngakhale zitavuta maka ngakhalenso moto umene amapanga nawo mwakutimwakuti monga mukumvera dzinalo.
Wotentha thupi sayandikira ngombe Mkazi amene thupi lake ndi la moto akuti sayenera kuyandikira ngombe kapena khola lake kuopetsa kuzibalalitsa chifukwa thupi lake ndi la moto. Izi ndimalinga ndi zikhulupiriro za Angoni ena achigawo chapakati koma kumva kwa ena kuchigawo cha kumpoto kwa dziko lino akuti mkazi sayandikira ngombe kuopetsa kuti asulutsa zizimba pakholalo.
Tidacheza ndi nyakwawa Chimpeni ya kwa T/A Phambala mboma la Ntcheu. Iye adati thupi la mayi amene adathera msinkhu ndipo wayamba kukhala kumwezi limakhala loopsa ku ngombe.
Iye adati mayi ameneyu saloledwa kuti adutse pakati pa ngombe zija zikamayenda kapena zikamawetedwa. Salolanso kuti alowe mkhola lake. Sangazikuse, sangakame kapena kutsekera pakhomo. Sangalowe mkhola ngakhale kukachotsa ndowe.
Nyakwawayi idati imakhulupirira kuti ngombezo zimabalalika ndipo zimayamba kugona mthengo.
Kusakatula malongedwe a ufumu wa Chitumbuka Apa tidacheza ndi nyakwawa Chibochaphere, ku Nkhamanga Kingdom mboma la Rumphi atangolongedwa ufumu.
Iye adati polonga ufumu wa Chitumbuka, pamakhala timiyambo tina tomwe wolongedwa ufumu ayenera kutsata. Choyamba, dzina likadziwika la amene alowe ufumu, dzinalo limayenera lipite kwa Sawira Chikulamayembe kuti akalivomereze. Monga mwamwambo, kwa Sawira supita chimanjamanja koma kukwapatira kangachepe mmanja. Kumeneko timati kuluvya pa Chitumbuka.
| 15 |
Papa Akana Kugona Hotela Yodula ku Mozambique Wolemba: Thokozani Chapola 9/06/Pope-in-Romania.jpg 301w" sizes="(max-width: 526px) 100vw, 526px" />Papa pa ulendo wake wa mmbuyomu Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse, Papa Francisco akuti wakana kukakhala ku hotela yapamwamba kwambiri paulendo wake wamasiku atatu ocheza mdziko la Mozambique mwezi ukudzawu.
Wailesi ya Vatican kulikulu la mpingowu, yagwira mau a Bishopu Antonio Juliasse Ferreira Sandramo wakulikulu-lo, yemwe wanena kuti mtsogoleri wa mpingo wakatolikayu, wakana ndandanda wa mahotela a pamwamba omwe akulukaulu omwe akuyendetsa dongosolo laulendowu mdziko la Mozambique, anatumiza ku likululo kuti nthumwi za papa pa ulendowu zisankhe, ndipo ati Papa, sakufuna malo apamwamba kwambiri.
Papa akuyembekezeka kukayendera dziko la Mozambique kuyambira pa 4 mpaka pa 6 mwezi wa mawa.
| 13 |
Zaka zinayi kwa ofuna kuba alubino Njonda ziwiri zochokera mboma la Mzimba Lachitatu zidagamulidwa kukasewenza jere kwa zaka zinayi ndi kugwira ntchito yakalavula gaga chifukwa chofuna kuba ndi cholinga chopha mwana wa chialubino wa zaka zinayi wa mwamuna.
Lusungu Sele wa zaka 30 ndipo amachokera mmudzi mwa Mkoko, T/A Chindi ndi Jailosi Luwanda wa zaka 24, wochokera mmudzi mwa Vakalani kwa Senior Chief Mtwalo adanyengerera bambo womupeza wa mwanayo kuti amube pamtengo wa K20 miliyoni.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Koma bwalo la milandu la Mzuzu pa 21 Decemberlidamasula bamboyo, Christopher Kumwenda wa zaka 38 yemwe amachokera mmudzi mwa Kumwenda, T/A Mzikubola mboma la Mzimba, ati popeza padalibe umboni wokwanira woti adali ndi cholinga chogulitsa mwana wake womupezayu.
Apa nkhaniyi idatsalira Sele ndi Luwanda.
Ndipo wapolisi woimira boma pamilandu Lloyd Magweje adauza bwalolo kuti Sele adalumikizana ndi Luwanda yemwe amakhala ku Mzuzu kuti ndiye adzagule mwanayo diluyo ikatheka.
Bwaloli lidamva kuti mphepo za chiwembuchi zitamupeza mayiyo adathawitsa mwana wakeyu kupita naye mmudzi mwa Chisewe, mboma lomwelo.
Koma pa 25 August chaka chatha, Sele adatsatira mwanayu mmudzimu pomwe adali kusewera pagulu la anzake.
Apa diluyo idapheduka popeza Sele adayamba wafunsa wachibale wa mwanayo za momwe angamupezere; ndipo wachibaleyu adakatsina khutu mayi wa mwanayo yemwe adakanena kupolisi kuti akusakidwa.
Ndipo Magweje adapempha bwaloli kuti liwapatse awiriwa chilango chokhwima chifukwa milandu yotere ikuchulukira komanso mwanayo adasiya kusewera ndi anzake ndipo amatsekeredwa mnyumba.
Podandaula, Sele adauza bwalolo kuti limupatse chilango chozizira poti amasamala banja lake pamene Luwanda adati ndi wamasiye komanso amasamala mkazi ndi ana ake awiri.
Poweruza, majisitileti Tedious Masoamphambe adati chilango chomwe abwalo amayenera kupereka chimafunika chikhale choti anthu akhutitsidwe nacho kuti chithandiza kuteteza ma alubino omwe akuphedwa ndi kuchitidwa nkhanza.
Masoamphambe adati komabe chilangochi chimafunika chikhale chogwirizana ndi mlandu kuti anthu asaganize kuti awiriwa alangidwa mwankhanza.
Ndili ndi chikhulupiliro kuti chilangochi chiwasintha kukhala nzika zabwino, Masoamphambe adatero asadapereke chigamulocho.
Koma chigamulochi sichidasangalatse bungwe loona za ufulu wa alubino la Association of People with Albinism in Malawi.
Mtsogoleri wa bungweli Bonface Massa adati akadakonda akadapatsidwa zaka zosachepera 14.
| 7 |
Njovu ipha mlenje Tsoka sasimba. Akanadziwa mlenje sakadapita kunkhalango ya Liwonde kukasaka nyama mozemba masiku apitawo.
Patrick Maya, wa zaka 52, ndipo amachokera mmudzi mwa Chipala, Senior Chief Kawinga mboma la Machinga, koma adasamukira mmudzi mwa Wadi, Senior Chief Liwonde komwe amakhala ndi banja lake adafa njovu itamuponda.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Malinga ndi mchimwene wa Maya, Maxwell Makina, iye adali ndi chizolowezi chosaka nyama mozemba pogwiritsanso ntchito agalu ake mnkhalango ya Liwonde.
Makina adati pa tsiku la tsokali, Maya adalowa mkhalangoyi komwe sadabwererenso.
Iye adati ngakhale nkhani ya kusowa kwake idawapeza abalewa mmudzi mwa Chipala laMulungu lapitali, akukhulupilira kuti mlenjeyu adaphedwa pa Khirisimisi.
Thupi lake lidapezeka Lamulungu pa 27 December, litaonongeka kale moti tidangosunga patchire pomwepo, Makina adatero.
Wachiwiri kwa mneneri wapolisi kuchigawo cha ku mmawa Otilia Kumanga watsimikiza za imfayi.
| 18 |
Chimulirenji Apempha Boma, Mipingo Ziyendere Limodzi Wolemba: Thokozani Chapola /wp-content/uploads/2019/09/chimulirenji.jpg" alt="" width="456" height="340" />Wapempha mgwirizano wa boma ndi mipingo-Chimulirenji Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino EVERTON CHIMULIRENJI wati boma ndi mipingo zikuyenera kugwirana manja potukula dziko lino.
CHIMULIRENJI amalankhula izi lero ku St. Lukes College of nursing ku MALOSA mboma la ZOMBA pa mwambo wopereka ma diploma a unamwino komanso uzamba kwa anthu okwana 176 omwe atsiriza maphunziro awopa college-yi. Iwo ati boma liwonetsetsa kuti ophunzira omwe akutsiriza maphunziro awo azipeza ntchito mosavuta. Ubale wa boma ndi mpingo ndi wa kalekale ndipo ndi omwe amatithandiza kukwaniritsa masomphenya athu ena. Choncho tikupempha kuti ubale umenewu upitilire kuti chitukuko chipite patsogolo, anatero a Chimulirenji.
Mmawu ake bishop wa Anglican mu dayosizi ya Uppershire BRIGHTON MALASA wati ali ndi chikhulupiliro kuti anamwino ndi azamba atsopanowa akagwira ntchito yawo moyenera.
Tawaphunzitsa mokwanira komanso moyenera ndipo ndi chiyembekezo chathu kuti akagwira ntchito ytawo moyenera mmadera muli monse momwe akuyembekezeka kukagwiramo ntchito, anatero bishop Malasa.
| 11 |
Atolankhani a Radio Maria Alandira Maphunziro Apadera Wolemba: Glory Kondowe 2/pagina-news-ed-eventi.jpg 2000w" sizes="(max-width: 505px) 100vw, 505px" />Phiri: Maphunziro ayenda bwino kwambiri Maphunziro apadera a anthu otumikira ku Radio Maria Malawi akuti ayenda bwino.
Mkulu woyendetsa ntchito za Radio Maria malawi a Louis Phiri ati maphunzirowa anakonzedwa ndi cholinga chofuna kusula mwa ukadaulo awulutsi komanso atolankhani a wailesiyi kuti ntchito zawo zipite patsogolo. Iwo ayamikiranso anthu omwe anaphunzirapo pa sukulu ya ukachenjede ya Polytechnic omwe ndi a mpingo wa katolika podzipereka kudzachititsa ma phunzirowa .
Maphuziro amenewa awathandiza anthu wotumikila pa Radio Maria Malawi kuti ntchito zawo zipite patsogolo makamaka pankhani yolemba ndi kuwerenga nkhani.
Tikuthokodzaso akhristu achikatolika omwe anaphunzirpo pa sukulu yawukachenjede ya polytechnic omwe anachiwona chopambana kuti azathandize wailesiyi ndi luso lawo pankhani yakulemba nkhani komanso kuwulutsa mawu ndinso momwe woyanganila ma studio angalembere ma lipoti awo, anatero a Phiri.
Mbali imodzi ya maphunzirowo Mmodzi mwa anthu omwe anaphunzirapo pa sukulu ya ukachenjede ya Polytechnic omwe ndi a mpingo wakatolika a Augustine Mlomole anati anawona kuti atha kuchitapo kanthu pothandiza Radio Maria Malawi ndi maphunziro ngati njira imodzi yomwe amafuna kukumbutsa ndinso kudziwitsa momwe angalembere nkhani komanso kuwelenga.
Iwo akuwona kuti achinyamata aku Radi Maria Malawi ali ndi chidwi malingana ndimamfunso omwe amafusa nthawi yamaphunzirowa ndipo awalimbikitsa kuti apitilize mtima wozichepesa ndikufuna kudziwa zambiri. Iwo apempha anthu ena akufuna kwabwino kuti achiteponso kanthu pothandiza wailesiyi kuti ipitilize kufalitsa nthenga wabwino.
| 3 |
Mmodzi Wafa pa Ngozi Mboma la Ntcheu Munthu mmodzi wafa ndipo asanu ndi atatu (8) avulala modetsa nkhawa galimoto yomwe anakwera itagubuduka mmudzi mwa Bula, ku Nsipe mboma la Ntcheu.
Malingana ndi mneneri wa apolice mbomali Sub Inspector Hastings Chigalu wati galimotoyi yomwe imayendetsedwa a Enerst Chitamba a zaka 22 zakubadwa a mboma la mzimba, inanyamula anthu a mpingo wa CCAP 13 omwe pa nthawi-yi anali akuchokera ku maliro mboma la Chiradzulu.
Iye wati galimoto-yi itafika pamalowa inagubuduzika ndi mmodzi mwa anthuwa a Charles Bonongwe wa mmudzi mwa Mzonda mdera la mfumu yayikulu Chitukula mboma la Lilongwe ndi amene wamwalira pa ngoziyi pomwe ena asanu ndi atatu avulala ndipo ayamba kulandira thandizo pa chipatala cha Ntcheu.
| 14 |
Dovu lakula ku nsanje Anthu ena mboma la Nsanje alephera kupirira nkhuli ndipo akuphabe ndi kugulitsa nyama ya ngombe, mbuzi, nkhumba ndi nkhosa mozemba motsutsana ndi chiletso chomwe unduna wa zamalimidwe udakhazikitsa pofuna kuthana ndi matenda a zilonda za mmapazi ndi mkamwa (foot and mouth disease) omwe adabuka mbomalo miyezi itatu yapitayo.
Escom in free-for-all fuel scam Wait gets longer Secrecy over party funders Unduna wa zamalimidwe udaletsa kupha kapena kugulitsa ziwetozi mbomali pa 8 January malinga ndi kubuka kwa matendawo, koma ngakhale chiletsochi sichidachotsedwe, anthu ena akuphabe ngombe ndi ziweto zina ndi kugulitsa nyama mozemba, zomwe zikupereka chiopsezo kuti matendawo atha kukhodzokera maboma ena.
Senior Chief Malemia wa mbomali watsimikiza kuti izi zikuchitikadi ndipo wauza achitetezo mmidzi kuti agwire aliyense amene amupeze akuchita izi.
Malire a Nsanje ndi Chikwawa amayenera kuponda mankhwala Vuto lake anthuwa akumapha ziweto mozemba, ndiye zikuvuta kuti tiwagwira bwanji, komabe tikuwafufuza ndipo tikawapeza tiwagwira, adatero Malemia.
Pocheza ndi Msangulutso palamya posachedwapa, Ernest Msambo wa ku Fatima kwa T/A Mlolo mbomalo adavomereza kuti kumeneko anthu akupha ziweto ndi kugulitsa nyama yake motsutsana ndi chiletso cha boma.
Achimwene, lija nkale adaletsa kuti anthu azipha ndi kugulitsa nyama, nkhuli yavuta, komanso anthu a kuno timadalira kupha kapena kugulitsa ziweto kuti tipeze ndalama, nchifukwa chake anthu akuchita izi mwakabisira. Pamsika nyama sungaipeze, koma mupeza mmakomo anthu akudya nyama, adatero Msambo.
Koma yemwe akulondoloza momwe nthendayi ikuyendera, Dr. Patrick Chikungwa, adati uku nkulakwa ndipo ngati anthuwa samvera lamulo la boma matendawa atha kufalikira dziko lonse.
Panopa tili mkati mothana ndi matendawa, ndiye ngati ena akuchita zithu mosemphama ndi ndondomeko yomwe takhazikitsa, asokoneza zomwe tikuchita. Adziwe kuti matendawa angathe kufalikira dziko lonse ngati anthu akuzembetsa ziweto kapena nyama pogwiritsa njira zamadulira, adatero Chikungwa.
Maboma ena monga Blantyre, Zomba, Mwanza, Mulanje ndi Thyolo kuchigawo cha kummwera amadalira nyama yochokera mboma la Nsanje ndi Chikwawa.
Malire a bomali ndi Chikwawa pa Sorjin komanso pa Phokera ndi Mtayamoyo paikidwa zipata za mankhwala a madzi omwe munthu aliyense ngakhale galimoto ikamatuluka mboma la Nsanje, akumapondapo kuti asalowetse matenda mmadera ena.
Koma Chikungwa wati izi sizingathandize kwenikweni ngati ena akudzerabe njira zina osadzera pazipatazi.
Apapa ndiye kuti angathe kulowetsa nyama mmaboma ena podutsa njira zachidule. Ikalowa mmadera ena ndiye kuti nakonso kufika matendawa ndiye kuthana nawo kwake kudzakhala kovuta kwambiri, adatero Chikungwa.
Iye adati kufika lero, achita katemera katatu mbomalo ndipo akudikira kuti aonetsetse ngati nthendayi yatheratu asadalengeze kuti anthu ayambe kupha ndi kugulitsa ziweto zawo.
Matendawa amapha ngombe koma nanga nchifukwa chiyani aletsanso kuti nkhosa, nkhumba ndi mbuzi zisamaphedwe? Nzoonadi, kuti matendawa amagwira maka ngombe, koma ziweto zinazi zili ndi kuthekera kofalitsa matendawa. Mwachitsanzo, nkhumba ndi imene ili pachiopsezo chachikulu kufalitsa matendawa.
Pofuna kuti matendawa tiwamalize mosavuta, tidaletsadi kuti ziweto zinazi zisatuluke mbomalo komanso zisaphedwe ncholinga choti pasakhale kufalikira kwa matendawa, adatero Chikungwa.
Iye adati ngombe ikagwidwa ndi matendawa, imatenga sabata ziwiri kuti iyambe kuonetsa zizindikiro zoti ikudwala. Ikagwidwa ndi zilonda za mmapazi komanso kukamwa imalephera kuyenda ndi kudya ndipo zikatero imafa.
Malinga ndi ofesi ya ziweto muunduna wa zamalimidwe, boma la Nsanje lili ndi ngombe 40 000, mbuzi 147 000, nkhosa 3 000 ndi nkhumba zoposa 20 000.
Boma la Chikwawa nalo lidakhudzidwa ndi matendawa ndipo ngombe 91 965 ndizo zidalandira katemera mchigawo choyamba cha katemerayo.
| 15 |
Anthu Awiri Afa Atamira Mmadzi ku Ntchisi Anthu awiri akuti apezeka atafa pa ngozi yomira mmadzi mboma la Ntchisi.
Malingana ndi wofalitsa nkhani za apolisi mbomalo Sub Inspector Richard Kaponda, ngozi yoyamba idachitika pa 7 May pomwe mwana wa miyezi 6 adapezeka atafa atagwera mmadzi omwe anali mu beseni , ndipo izi zinachitikira mmudzi wa Mwamulo, mdera la mfumu yayikulu Malenga mbomalo.
Munthu wina amene wakhudzidwanso ndi imfa ya mtunduwu ndi bambo wina wamisala yemwe sakudziwika kwawo ndipo anapezeka atafera mu mtsinje wa Mdambo umene ukupezekanso mmudzi mwa Mdambo mdera la mfumu yayikulu Malenga mboma lomwelo la Ntchisi ndipo izi zinachitika pa 8 mwezi omwe uno.
Mwazina Sub-Inspector Kaponda wapempha anthu omwe ali ndi ana komanso anthu omwe ali ndi vuto la mu ubongo kuti aziwayanganitsitsa zomwe akuchita pofuna kupewa imfa za mtunduwu.
| 14 |
Chilonda chatukusira mu DPP Bwerani poyera mulankhule kwa Amalawi. Awa ndi mawu a akadaulo pa ndale pamene alangiza mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika ndi wachiwiri wake Saulos Chilima kuti alankhulepo pa mpungwepungwe omwe wabadwa mchipanicho.
Akadaulowo, Emily Kamanga ndi Henry Chingaipe alangiza izi kutsatira kusamvana pa yemwe atengere chipanicho kuchisankho cha 2019.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Chilima ndi Mutharika Msabatayi, anthu akhala akubwera poyera ndi zovala za DPP zokhala ndi nkhope ya Chilima kuti ndiye atengere DPP kuchisankho cha 2019.
Koma Lolemba, mlembi wa chipanicho Grelzedar Jeffrey adatsindika kuti zovalazo si za DPP chifukwa zovala zawo zimakhala ndi nkhope ya Mutharika kapena mkulu wake Bingu yemwe adayambitsa chipanicho.
Tikudziwa akupanga izi ndi adani athu, kotero dziwani kuti chipani chili ndi mphamvu kulanda zovala zimenezo. Zovala za DPP zimakhala ndi nkhope ya yemwe adayambitsa chipanichi Bingu wa Mutharika kapena amene ndi mtsogoleri pano, adatero Jeffrey.
Iye adaopseza: Titengera kukhoti aliyense amene akugawa kapena kupanga zovalazo.
Koma mmodzi mwa anthu amene sakufuna Mutharika, Bon Kalindo wati iye pamodzi ndi gulu lawo sabwerera ndipo sachita mantha pokhapokha Chilima akhale pachiongolero.
Sabata yatha, anthu adadzidzimuka pamene adamvetsera uthenga womwe Jeffrey amalankhulana ndi nduna ya maboma angono KondwaniNankhumwa.
Mzolankhula zawo, Jeffrey adaulula kuti Chilima sakubwerera ngakhale Mutharika amulonjeza zokhalanso wachiwiri wake.
Ineyo ndidalankhula naye [Chilima] koma adanditsimikizira kuti sakufuna kukhala wachiwiri kwa Mutharika ngakhale kumsonkhano waukulu sadzapitako ati angokhala.
Ndinadabwa kuti basi angokhala? Ndiye ineyo ndi wandale ndikudziwa chomwe akutanthauza, adatero iye.
Bwana ndakhala ndikukuuzani, wamisala adaona nkhondotu. Chilichonse chimene ndakhala ndikulankhula ndi chomwe chikuchitika. Anthuwatu adayamba kale.
Ndidakuuzani kuti Chilima sabwereranso ndipo akupanga zake. Anthu awa bomali alilowerera. Ngakhale bwana [Mutharika] atani maka Chilima salola. [Noel] Masangwi sabwereranso. Bwana aitanitse NGC, chifukwa kumsonkhano waukulu Chilima sangawine. Akulimbana ndikugawa DPP cholinga MCP itole boma, adatero mlembiyu.
Mkamanga akuti chofunika nchoti Mutharika komanso Chilima abwere poyera ndi kulankhula kuti zonsezi zitheretu.
Nkhani yonseyitu ikukamba za awiriwo, ndiye ngati atalankhula, zonse zingathe. Komabe ndilibe chikhulupiriro ngati awiriwo amalankhulana. Apapa zavuta basi ndipo ndikukaika ngati angamvane, adatero Mkamanga.
Naye Chingaipe adati kusalankhula kwa awiriwo ndikomwe kukuze bala la chipanicho kotero ayenera abwere poyera.
| 11 |
Blantyre yawala, iwalirabe Kuyenda usiku tsopano sikukhalanso koopsa ganizo la khonsolo ya mzinda wa Blantyre lipherezeke.
Mneneri wa khonsoloyi, Anthony Kasunda, wati khonsolooyi ikuganiza zoika magetsi mmisewu kuti aziwala usiku wonse mumzindawu.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mmbuyomu ena adaba zitsulo za magetsi Kasunda wauza Tamvani kuti pasadathe miyezi 6 msewu wa Masauko Chipembere Highway ukhala ndi magetsiwa kuchoka ku Blantyre mpaka ku Limbe.
Anthu aona kuwala ndithu. Ife talowa mumgwirizano ndi bungwe la Roads Fund Administration kuti tigwire ntchito imeneyi, yomwe idye ndalama zokwana K400 miliyoni, adatero Kasunda.
Iye adati mmisewu ina ingapo ntchitoyi yagwirika kale.
Tapanga kale kuchoka pa Kandodo Corner Shop mpaka pa Kameza Roundabout; Kwacha Roundabout mpaka pa Kudya kudutsa MBC TV, CI mpaka Green Corner; ndinso Sunnyside mpaka ku Manyowe.
Ntchito imeneyi yatitengera ndalama pafupifupi K145 miliyoni, zomwe ndi gawo la K1.8 biliyoni zochokera kuboma za ntchito yachitukuko cha mumzinda wa Blantyre, adatero Kasunda.
Mneneriyu adatinso khonsolo ikamapeza ndalama, ionetsetsa kuti misewu yonse ya mumzinda wa Blantyre ikhale ndi magetsi.
Magetsi amathandiza kukhwimitsa chitetezo. Ndikhumbo la khonsolo ya Blantyre kuti mzinda ukhale wowala usiku. Tikumema anthu onse a mumzindawu kuti atithandize poteteza magetsi amenewa, makamaka potsina khutu apolisi kapena akulu a khonsoloyi akaona wina akuononga dala zipangizo zamagetsi monga mapolo ndi nthambo zamagetsi, adaonjezera Kasunda.
| 15 |
Papa Wasankha Archbishop Giordana Kuti Awunike Ofesi Ya Tchalitchi Cha St. Peters Basilica Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wasankha mkulu woti awunike momwe ofesi yomwe imayanganira tchalichi lalikulu la Saint Peters Basilica izigwirira ntchito zake.
Malinga ndi malipoti a Vatican Radio, Papa wasankha Archbishop Mario Giordana kuti agwire ntchitoyi.
Malipoti akuti mwazina Archbishop Giordana awunika malamulo omwe ofesi yomwe imayanganira tchalichi lalikulu la Saint Peters Basilica izigwiritsa ntchito.
Archbishop Giordana agwira ntchitoyi ngati Commissioner wapadera (Extraordinary Commissioner) mothandizana ndi bungwe lomwe alikhazikitse Ofesi yomwe imayanganira tchalichi lalikulu la Saint Peters Basilica amayitchula kuti the Fabric of Saint Peter kapena kuti Fabbrica di San Pietro ndipo zina mwa ntchito zake ndi kuonetsetsa kuti tchalitchi la Saint Peters Basilica likusamalidwa bwino komanso kukonza zomwe sizili bwino mtchalichili (maintainance).
Lolemba pa 1 June 2020 likulu la mpingo wa katolika ku Vatican linatulutsa kalata yonena za lamulo la tsopano lomwe Papa Francisco adakhazikitsa lothandiza kuteteza chuma ku likulu la Mpingowu komanso momwe ma kampani ogwira ntchito ndi likulu la Mpingowu azisankhidwira.
Malinga ndi kalatayo ma kampani ofuna kugwira ntchito ndi likulu la Mpingowu azipikisana ndipo azisankhidwa potsata ndondomeko zokhazikika ndipo izi zizichitika poyera popewa chinyengo china chilichonse.
Likulu la Mpingo wa Katolika, Vatican, lomwe ndi dziko loima pa lokha linakhazikitsa lamuloli lomwe lili ndi mitu 86 mogwirizana ndi mfundo za bungwe la United Nations zolimbina ndi mchitidwe wa ziphuphu ndi katangale.
| 13 |
Tidangoonana koyamba basi Kukumana kudziko la eni nkudziwana kuti mumachokera kumodzi ndi chinthu chonyaditsa kwambiri moti kwa anthu ena chinansi chimayambira pomwepo ngakhale atakhala kuti amachokera mzigawo zosiyana kwawoko.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Nkhani yathu lero ndi ya Wonder Msiska, wochokera mboma la Karonga yemwe akugwira ntchito kuwayilesi ya Staryomwe idaphathikana ndi kanema ya Timveniyemwe pano ali pabanja ndi Hazel Silekile, naye wa ku Karonga, ndipo akugwira ntchito kukampani ya BETAMS Ltd.
Sadzalekana: Wonder ndi Hazel kutsimikiza kuti ali thupi limodzi Awiriwa adakumana ku Britain mchaka cha 2008 komwe onse adapitira maphunziro ndipo adakaphana maso kumwambo wa chinkhoswe cha Mmalawi wina wake nkukondana pomwepo.
Zidangochitika kuti takondana basi. Ndikhulupirira ndi momwe Mulungu adakonzera. Choyamba, tonse tidapitira maphunziro kenako nkuganiza zopita kumwambo wa chinkhoswe komwe tidakakumana, adatero Wonder.
Iye adati atakumana kuchinkhosweko sipadatenge nthawi kuti ubwenzi uyambe mpaka kugwirizana za banja komweko.
Kusiyana ndi ena omwe amadikira tchuthi kuti akapange chinkhoswe kwawo, Wonder ndi Hazel akuti chinkhoswe chawo chidachitikira ku Mangalande komweko ku Sutton Coldfied mchaka cha 2009.
Si kuti udali mwano kapena kudzitama, ayi, koma tinkafuna kuti timaliziretu zomwe tidapitira kumeneko komanso panthawi yomweyo tionetse kuti tidakondanadi. Titabwerera kumudzi ku Malawi mpomwe tidayamba za mwambo waukulu wa ukwati, adatero Wonder.
Ukwati wa awiriwa udachitikira mumzinda wa Blantyre mchaka cha 2012 atabwerako ku Mangalande ndipo pano ali ndi mphatso ya ana aakazi awiri.
Wonder adanenetsa kuti atakhalanso ndi mwayi wina wosankha wachikondi akhoza kubwereza chisankho chake chifukwa iye mtima wake udakhazikika pa Hazel ndipo ndi khumbo lake kudzasungana naye mpakana kalekale.
Hazel adati kwa iye Wonder ndiye mbali imodzi ya thupi lake ndipo sangagwedezeke ndi chilichonse chifukwa mwa iye adapeza mwamuna wachikondi ndi wachilungamo.
Akuti iye akakhala, kaya nkutchito, pakhomo ngakhalenso kunyumba saona chomulekanitsa ndi mwamuna wakeyu ndipo naye ali ndi chiyembekezo cha banja lapamwamba ndi lotsogola komanso latsogolo lowala.
| 15 |
Chisankho chachibwereza chilipo pa 6 June Bungwe loyendetsa zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) lakhazikitsa pa 6 June 2017 kuti Amalawi adzaponye voti yachibwereza kummwera cha kummawa kwa Lilongwe patangotha mwezi bwalo lamilandu la apilo litagamula kuti chisankho cha kuderali sichidayende bwino.
Chigamulochi chidaperekedwa potsatira dandaulo la yemwe ankaimira chipani cha Malawi Congress Party (MCP) Ulemu Msungama kuti chinyengo chidachitika pachisankhocho.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Voters will still use voter ID cards in 2019 Chigamulochi chitaperekedwa, zipani zandale zidapempha MEC kuti ichititse chisankho chachibwereza kuderalo msanga kuti anthu akhale ndi phungu wowaimirira ku Nyumba ya Malamulo chifukwa chigamulocho chidatanthauza kuti deralo lilibe phungu.
Pachisankho cha pa 20 May, 204, MEC idalengeza kuti Bentley Namasasu wa Democratic Progressive Party (DPP) ndiye adapambana koma Msungama adakamangala ku bwalo la mirandu za chigamulochi.
Wachiwiri kwa mlembi wa chipani cha MCP Eisenhower Mkaka, mneneri wachipani cha Peoples Party (PP) Noah Chimpeni ndi mneneri wa United Democratic Front (UDF) Ken Ndanga adati MEC isapange chidodo pa zopangitsa chisankho chachibwereza.
Mobweretsa chilimbikitso pa nkhawa ya za vuto la ndalama zopangitsira chisankhochi lomwe bungwe la MEC lidanena poyamba, bungweri lati chisankhochi chilipo pa 6 June 2017.
Potsatila chigamulo cha bwalo la mirandu la apilo, bungwe la MEC lidapangitsa msonkhano pa 4 April omwe lidafotokozera zipani ndi okhudzidwa ena kuti lipangitsa chisankho ku dera la ku mmwera cha ku mmawa kwa Lilongwe pa 6 June 2017, chidatero chikalata chomwe bungweli lidatulutsa.
Chikalatachi chidatinso pofuna kuti bungweli lisawononge ndalama zambiri, chisankhochi chichitika limodzi ndi zisankho zina monga kumpoto kwa Lilongwe Msozi, chisankho cha khansala wa kumpoto kwa Mayani ku Dedza ndi khansala wa kwa Mtsiliza ku Lilongwe.
Bungwe la MEC lati makandideti akale ndi atsopano ndi olandilidwa kupikisana nawo motsatana ndi malamulo a zisankho.
Pa zisankhozi, bungwe la MEC lati omwe adzaloledwe kuponya voti ndi okhawo omwe adalembetsa mkaundula wa 2014 ndipo sipadzakhala zosintha malo okaponyera voti.
Zipani za MCP, PP ndi UDF zati nkhaniyi ndi yabwino koma zati mpofunika kuwonetsetsa kuti pasadzachitikenso zachinyengo zomwe zingadzapangitse kuti zotsatira za chisankhochi zidzakanidweso.
| 11 |
Ndimafuna mwamuna wadzitho Felix Mwamaso ndi mmodzi mwa akatswiri osewera nkhonya mdziko muno. Koma kuti zonse zizimuyendera tayale choncho pali nthiti yake, Queen, yemwe amamuchengeta. Koma nanga awiriwa adakumana bwanji? Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndinkafuna mwamuna wadzitho, nthawi zonse ndinali kudikirira kuti ndidzapeze wamaonekendwewa. Nditamuona Felix akuponya maso pa ine panthawi ya nkhonya yake ku Obrigado Leasure Park mumzinda wa Mzuzu, ndinati mwayi suposa apa, adatero Queen polongosola mmene adakumanirana koyamba ndi mwamuna wake.
Adayanjana magazi: Queen ndi Felix Mwamaso Kuchokera panthawi imene adaonana pamalo ankhonyawa mu August chaka cha 2013, awiriwa adagwa mchikondi chozama ndipo kenako adamanga banja chaka chomwecho mwezi wa November.
Malinga ndi maongokedwe ake, Queen adandipatsa chikoka choti ndimutengere panyumba. Mwamwayi nditaponya mawu oti ndamukonda sadavute, ndipo ndidazitenga kuti ndi zomwe amayembekezera, adatero Felix.
Awiriwa akukhalira limodzi ku tauni ya Chibavi ku Mzuzu.
Lachitatu sabata yatha, chisangalalo chokumbukira kuti akwanitsa zaka zitatu ali limodzi ngati banja chidali cha mtima bii ndipo chidachitikira pamalo ena achisangalalo ku Mzuzu otchedwa Sports Cafe.
| 15 |
Akapeza thanthwe pokumba manda zimatha bwanji? Zochitika kumanda nzambiri nthawi yokumba manda koma palibe nthawi yomwe adzukulu amakhaula kwambiri kuposa pamene apeza thanthwe dzenjelo lisadathe chifukwa sipakhala kusiya kuti akayambe pena. Uwu sumakhala ulesi, koma kuti ndi mwambo wake momwe zimayenera kukhalira. STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi gulupu Mtwambwa wa ku Lilongwe yemwe akulongosola za mwambowu motere: Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mtwambwa: Kumakhala ngati kuwayesa azimu Mfumu, tiuzeni kuti ndinu yani? Ndine Gulupu Mtwambwa ya mdera la T/A Kalumba ndipo mtundu wathu ndi wa Achewa.
Mfumu, kumanda kumachitika zambiri adzukulu akamakumba koma chidandipatsako chidwi nchakuti akapeza mwala, mmalo mokwirira nkukumba pena amapitiriza. Kodi nchifukwa chiyani? Ndi mwambo umene uja, sangayerekeze kusiya dzenje loyambayamba nkuyambiranso lina chifukwa akhoza kukhala ndi mlandu waukulu mmudzi moti akhoza kulipitsidwa chindapusa chachikulu kapena kusamutsidwa kumene mmudzi atapanda kugonjera chigamulo cha akuluakulu.
Ndi mlandu wanji umenewu? Umenewu ndi mlandu wolowetsa mphepo mmudzi. Ife timakhulupirira kuti kuyamba kukumba dzenje nkulilekeza panjira kuli ngati kukumba dzenje koma osaikamo maliro, zomwe zimapangitsa kuti anthu azipululuka chifukwa mizimu yakwiya kuti mwainamiza kuti kukubwera mmodzi mwa ana awo.
Si zongokhulupirira izi nanu Achewa? Si zongokhulupirira, ayi, zimachitika. Ngakhale mutayenda kuno mpaka kufufuza mmanda simungapeze dzenje loyamba kukumbidwa kapena lomalizika kukumbidwa koma losaikamo mtembo. Zimenezi sizingatheke ndipo mfumu ya mmudzi momwe mungachitike zotere yokha imadziwiratu kuti ikhoza kukhala pamoto waukulu.
Nanga thanthwelo likakhala lalikulu? Basi adzukuluwo adziwa momwe achitire koma dzenjelo lipitirire basi mpaka lithe. Uthenga ukamabwera kumudzi kuti nyumba yatha kumanda, likhale kuti dzenjelo lakwanadi monga ndi momwe chikhalidwe chimanenera.
Si chilango kwa adzukulu chimenechi? Ayinso, palibe za chilango. Kodi tiwalanga ngati abweretsa zovuta ndi iwowo bwanji? Munthu akamati akulowa mgulu la adzukulu, amadziwiratu ntchito yomwe azikagwira kumeneko ndiye zonsezi amazidziwa kale, sizikhala zachilendo akakumana nazo.
Kapenatu mwina mumaona kuti malo angamathe msanga? Ndinu nkhakamira. Moti monse muja simukumvabe kuti timatsatira mwambo momwe umayenera kukhalira? Ifensotu tidakhalako adzukulu ndipo zimenezi tidakumanapo nazo, sikuti zayamba lero. Tidazipeza, zikupitirira ndipo zidzakhalako mpaka kalekale.
Nanga akakhala kuti akumba poti padaikidwa kale munthu? Apa pokha akhoza kufotsera nkuyamba pena, koma kuti mafumu adziwitsidwe ndipo akhale ndi umboni. Nzosavuta chifukwa mizimu singakwiye poti nayo imadziwa kuti alakwitsa, pamalopo padali kale nyumba ya wina.
| 15 |
MEC igwira njakata pa zisankho zapadera Zinthu sizikuyenda kubungwe loyendetsa zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) komwe tsogolo la zisankho zapadera silikudziwika.
Lachitatu lapitali, mkulu wa nthambi yoona za chuma kubungweli, Linda Kunje, adauza Tamvani kuti zisankho zachibwereza zichitikabe mtsogolo muno koma tsiku lenileni silikudziwika.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mathanga: Tikudikirabe ndalama kuchokera kuboma Posachedwa bungwe la MEC lidatulutsa chikalata chodziwitsa onse okhudzidwa ndi zisankhozi kuti ayamba aziimitsa kaye kaamba koti boma silidapereke ndalama zoyendetsera zisankhozi, zomwe zikuyembekezeka kuchitika ku Mchinji West Constituency, Kaliyeka Ward ku Lilongwe City South East Constituency, Sadzi Ward ku Zomba Central constituency, Bunda Ward ku Kasungu Central Constituency ndi Bembeke Ward ku Dedza South Constituency.
Mmodzi mwa makomishona kubungweli, Jean Mathanga, akuti pakufunika zosachepera K499 miliyoni zoyendetsera zisankhozi.
Mathanga adati boma silidawapatse ndalamazo koma adatsimikiza kuti zisankhozi zichitikabe mtsogolo muno.
Koma mneneri wa nthambi yoona za chuma kuboma, Nations Msowoya, watsindika kuti boma silipereka ndalama ku MEC pokhapokha lipoti lofotokoza za kusokonezeka kwa ndalama kubungweli litatulutsidwa.
Msowoya: Boma silipereka msanga ndalama Ife tidapempha kuti pakhale kafukufuku pa momwe ndalama zidayendera ndipo chomwe tikudikira ndi lipoti. Akatipatsa lipotilo, ndipo tikakhutitsidwa nalo tikhala okonzeka kupereka ndalamazo, adatero Msowoya.
Mchaka cha 2012 mpaka 2014, kubungweli kudasowa ndalama zoposa K15 miliyoni. Kusowa kwa ndalamazi kudachititsa kuti akuluakulu ena kubungweli akakamizidwe kuti akapume kaye ndi cholinga choti afufuze bwino za mmene ndalama zosowazo zidayendera.
Pa 24 August chaka chino, MEC idatumiza akuluakuluwo, omwe ndi mkulu wa zisankho Willie Kalonga, komanso Harris Potani, George Khaki, Khumbo Phiri, Edington Chilapondwa, Chimwemwe Kamala, ndi Sydney Ndembe kuti abapuma kaye pomwe zofufuzazo zili mkati.
Zitachitika izi, mu August momwemo, boma lidalemba anamnadwa atatu, Rex Harawa, Stevenson Kamphasa ndi Duncan Tambala kuti achite kafukufuku pa kusokonekera kwa ndalamazo.
Koma izi zili chonchi, Kunje akuti zisankho zikhalapobe posakhalitsapa.
Mitima ya anthu ikhale mmalo. Ngakhale sitingalonjeze tsiku lenileni lomwe zisankhozi zidzachitike, zichitika ndithu posakhalitsa, adatero iye.
Si izi zokha, kumwaliranso kwa wapampando wa MEC, Maxon Mbendera, ndi komwe kukukayikitsa ngati bungweli lingapangitse zisankho posakhalitsa. Koma malinga ndi Kunje, ili si vuto.
| 11 |
Boma lalowa nthenya Mphunzitsi kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, Blessings Chinsinga, wati kumangidwamangidwa kwa anthu omwe akuoneka kuti siabwenzi a boma kukutanthauza kuti boma la DPP lachita mpungwepungwe kotero likungofuna kuthana ndi anthuwa.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Chinsinga adalankhula izi msabatayi kutsatira kumangidwa kwa yemwe akufuna kudzaimira ngati pulezidenti mchipani cha UDF mmasankho a mu 2014, Atupele Muluzi.
Kumangidwa kwa Muluzi kukutsatira kumangidwa kwa mkulu wa bungwe loona ufulu wa ogula la Consumers Association of Malawi (CAMA), John Kapito yemwe adatoledwa atapezeka ndi ndalama zakunja.
Apolisi adamanganso mkulu woimira anthu pamilandu, Ralph Kasambala pomuganizira kuti adavulaza anthu ena.
Chinsinga wati boma likuonetsa kuti lagwidwa njakata ndipo likungofuna kuthana ndi omwe akulijejemetsa zina.
Apa wina akangokalasula khala athana naye. Koma ndidakakonda [boma] likadasiya Amalawi kuti azilankhula zakukhosi kwawo popanda kukokana, akuganiza choncho Chinsinga.
Iye wati izi zingasiye Amalawi pamavuto chifukwa chilichonse chikuchitika Amalawi ndiwo akhale pamoto.
Kapito komanso Kasambala akhala akulankhula poyera kuti mtsogoleri wa dziko lino, Bingu wa Mutharika akuyenera akapume ponena kuti mavuto ali mdziko muno adza kaamba ka iye.
Atupele adanjatidwa Lachiwiri msabatayi ku Lilongwe akupita ku Blantyre.
Kumangidwa kwake kumadza pomwe apolisi adabalalitsa anthu Lasabata pa 18 mumzindawu pomwe mkuluyu amafuna alankhule nawo.
Iye adamusunga ku ndende ya Maula. Pomwe timalemba nkhaniyi Lachitatu nkuti Atupele atamutengera kuchipatala cha Lingadzi kaamba ka vuto lakuthamanga kwa magazi.
| 11 |
K5 biliyoni yothana ndi matenda a mkungudza Bungwe la Queen Elizabeth Diamond Jubilee Trust (QEDJT) lapereka ndalama zokwana K5 biliyoni kuboma la Malawi zogwirira ntchito yothetsa matenda a khungu otchedwa mkungudza (trachoma) mdziko muno.
Potsimikiza nkhaniyi, mneneri wa unduna wa zaumoyo, Adrian Chikumbe, wati boma ligwira ntchitoyi ndi mabungwe angapo, kuphatikizapo lodziwika bwino mdziko muno la Sightsavers, lomwe lidalandira ndalamazi.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Ntchitoyi, yomwe adaikhazikitsa kale mdziko muno mu October chaka chathachi mboma la Karonga, akuti idya ndalama zokwana K5.110 biliyoni mzaka zinayi zomwe akhale akuigwira.
Koma Chikumbe adauza Tamvani kuti ngakhale kuti dziko lonse la pansi laika 2019 ngati chaka chothetsera matendawa, boma la Malawi ligwira nchitoyi mwachangu komanso molimbika kuti pofika 2018 matendawa adzakhale atatheratu mdziko muno.
Nthawi yoti matendawa adzakhale atatheratu padziko lonse la pansi ndi chaka cha 2019, koma kuno ku Malawi taganiza kuti tichite chamuna pothana nawo chisanafike chaka chimenecho, adatero Chikumbe.
Mkuluyu adatinso pakalipano matendawa avuta kwambiri mmaboma okwana 15. Pachifukwachi, bungwe la Sightsavers akuti layamba kale kugwira ntchitoyi, maka mmaboma omwe akhudzidwawo.
Iye adati ntchito yogawa mankhwala kwa odwala nthendayi ifalikira madera onse a dziko lino posachedewapa ndi cholinga chothana ndi matendawa msanga.
Panopa, maboma omwe akhudzidwa kwambiri ndi nthendayi ndi a Kasungu, Nkhotakota, Salima, Karonga, Mchinji, Lilongwe, Zomba, Machinga, Mangochi, Ntcheu, Nsanje, Neno, Mwanza, Dowa ndi Ntchisi, adatero Chikumbe.
Nalo bungwe la Sightsavers, lomwe ndi akadaulo odziwa bwino za ntchitoyi, lati dziko la Malawi lili mgulu la maiko oyambirira okwana 14 padziko lapansi omwe akuvutika kwambiri ndi matenda a mkungudzawa.
Pafupifupi anthu okwana 230 miliyoni omwe akudwala matendawa padziko lapansi, 9.5 million ali ku Malawi, latero bungwe la Sightsavers.
Malinga ndi a Sightsavers, ntchitoyi akuti ikayambika agawa mankhwala kwa anthu oposa 8 miliyoni mdziko muno.
Mchikalata chake, bungweli lati matenda a mkungudza ngakhale kuti ndi ochizika, ndi osautsa kwambiri kotero kuti ngati munthu achedwa kulandira chithandizo msanga akhoza kupunduka ndi kukhala wakhungu.
Bungweli lati zina mwa zizindikiro za nthendayi ndi zakuti zikope nthawi zambiri zimagwera mkati mwa diso, kenaka nsidze zimayamba kukanda galasi la disolo mpaka kuchita zilonda. Ndipo zinthu zikafika pamenepo munthuyo sangathenso kuona.
Bungweli lati nthendayi, yomwe ndi yopatsirana, imafala mofulumira ngati anthu ambirimbiri akhala malo othinana, komanso opanda ukhondo wokwanira.
Malinga ndi a Sightsavers, bungwe la zaumoyo padziko lonse la pansi la World Health Organisation ndi lomwe lidavomereza kuti ntchito yotereyi ichitike ndipo maiko ena omwe ntchito yamtunduwu ichitikenso ndi Kenya, Uganda, Nigeria ndi Mozambique.
| 18 |
Papa Wati Kukambirana ndi Njira Yodzetsera Mtendere Wolemba: Glory Kondowe Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisko lero wati kukambirana ndi kumvetserana ndi njira yokhayo yothetsera kusamvana.
Papa Francisko Papa Francisco amalankhula izi pa misa ya mmawa ku likulu la mpingowu ku Vatican.
Iye wati msonkhano wa ku Yerusalemu mbukhu la Ntchito za atumwi, ndi chitsanzo chabwino pofuna kuthetsa mikangano ndi kusamvana komwe kungakhalepo pakati pa anthu masiku ano.
Papa wati nthawi zonse pamene pali mikangano ndi kusamvana anthu akuyenera kudalira Mulungu pobwera pamodzi kukambirana, kumvetserana ndi kuchita zinthu zokondweretsa Mulungu.
| 14 |
Avulaza shehe akuitanira mapemphero Nthawi ikamathamangira 5 koloko mmawa, anthu achipembedzo cha Chisilamu amadzutsidwa kuti akachite mapemphero kumzikiti pamene shehe kapena mwazini (muezzin) amakhala akukuwa.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Koma zachitika ku Nkhotakota si ndizo komwe anthu achiwembu avulaza shehe amene amaitanira mapempherowo.
Ali mu ululu: Shehe Ainani kulandira chithandizo mchipatala Mneneri wa polisi ya Nkhotakota, Williams Kaponda, wati izi zidachitika mmawa wa Lachitatu lapitali ndipo sheheyu adamugoneka mchipatala cha Nkhotakota.
Kaponda adati sheheyu dzina lake ndi Namandwa Ainani, wa zaka 57, amene akuchokera mmudzi mwa Malenga kwa Senior Chief Malengachanzi mbomalo.
Ainani adadzuka mmawa pamene amamemeza anthu achipembedzo cha Chisilamu kuti adzuke akapemphere kumzikiti wa Malenga.
| 13 |
Pasakhale Oponya Voti Atsopano-Supreme Court Bwalo la Supreme lagamula kuti chisankho chatsopano cha president chichitikebe mdziko muno popanda anthu atsopano kutenga nawo gawo pa chisankhochi.
Bwaloli lanena izi mu chigamulo chake pomwe bungwe la MEC komanso chipani cha DPP anakasuma potsutsana ndi chigamulo chomwe bwalo la za malamulo linapereka kuti chisankhochi chichitike mmasiku 150 kuyambira pa 3 February chaka chino.
Bwaloli lati anthu amene anaphwanyiridwa ufulu ndi amene anavota pa chisankho cha chaka chatha choncho palibe chifukwa choti anthu ena atsopano alembedwenso mu kaundula wa voti-yi.
Tawamenya 6-0 chifukwa adabwera koyamba kuti ayimitse mlandu anamenyedwa, ku constitution khoti anawakana ndipo apanso chimodzi modzi, anatero Chilima.
Iwo ati bwalo la mlanduli lagamulanso kuti onse omwe atakaponye voti ndi omwe analembetsa chaka chatha komanso anthu omwe atapikisane ndi omwe anali pa mndandandawu chaka chatha koma iwo ati sakubwelera mmbuyo ndipo apitilira kuyenda limodzi ndi a Lazarus Chakwera a chipani cha MCP pa mlanduwu.
Mchigamulocho bwaloli lalamula bungwe la MEC kuti libwenze ndalama zonse zomwe odandaula omwe ndi zipani za MCP ndi UTM, zawononga kuchokera pa chiyambi cha mlanduwu.
| 11 |
Amayi Ozembetsa Mankhwala Ozunguza Bongo Apatsidwa Chilango Wolemba: Thokozani Chapola wp-content/uploads/2019/10/ADARKWA.jpg 607w" sizes="(max-width: 282px) 100vw, 282px" />Amulamula kuti akagwire ukayidi ku Maula kwa zaka ziwiri-Adarkwa Bwalo la milandu la Mkukula ku Lumbadzi mboma la Dowa lachitatu lalamula amayi awiri kuti akakhale ku ndende ndi kukagwira ukayidi atapezeka olakwa pa mlandu wofuna kuzembetsa mankhwala ozunguza bongo otchedwa Apomorphine.
Amayi awiriwa Harriet Namate wa mboma la Zomba komanso Sally Adarkwa yemwe ndi mzika ya dziko la Ghana anagwidwa sabata ziwiri zapitazo pa bwalo la ndege la Kamuzu mu mzinda wa Lilongwe.
Wofalitsa nkhani za apolisi ku bwalo la ndege la Kamuzu Sub Inspector Sapulani Chitonde wati Namate yemwe anapezeka ndi mankhwalawa olemera 7 kilograms amulamula kuti akagwire ukayidi kwa zaka zitatu ndi theka ndipo Adarkwa yemwe anapezeka ndi mankhwalawa olemera 5 kilograms amulamula kuti akagwire ukayidi kwa zaka ziwiri.
Ngakhale awiriwa kudzera mwa ma lawyer awo anapempha bwaloli kuti liwamvere chisoni kaamba koti ndi amayi komanso amachita kutumidwa ndi abambo ena, bwaloli linawona kuti mkofunika kuti awiriwa apatsidwe chilango cha mtunduwu kaamba koti ati mchitidwewu ukuchulukira mdziko muno.
Padakalipano Chitonde wati bwalo la ndege la Kamuzu si malo ophweka podusitsira mankhwala ozunguza bongo ndipo anthu akuyenera kupewa kuchita izi.
| 7 |
Mutharika Walamula Unduna Ulembe Ntchito Anthu Azachipatala 2000 Mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika walamula unduna wa zaumoyo kuti ulembe ogwira ntchito owonjezera mzipatala okwana 2000, pofuna kuwonetsetsa kuti anthu akulandira thandizo la chipatala mosavuta.
Walengeza ndondomeko zatsopano-Mutharika Mutharika wanena izi lachisanu pomwe amalengeza ndondomeko zatsopano zopewera matenda a COVID-19 pomwe tsopano zadziwika kuti anthu anayi ali ndi kachilombo ka Coronavirus mdziko muno.
Mwazina Mutharika walamulanso bungwe la MERA kuti litsitse mtengo wa mafuta a galimoto, pofuna kuti mtengo womwe anthu akulipira poyenda maulendo utsike.
Izi zikutsatira dongosolo lomwe boma linakhazikitsa lochepetsa anthu okwera galimoto pofuna kupewa kukhudzana kwa anthu komwe kungatichitse kuti apatsirane kachilombo ka Coronavirus mosavuta, zomwe zinachititsa kuti eni minibus akweze mitengo yawo.
Padakalipano zadziwikanso kuti mwa anthu anayi omwe apezeka ndi Coronavirus mdziko la Kenya, awiri mwa iwo anafika mdziko muno asanafike mdzikolo.
| 11 |
Ulangizi paulimi mu 2016 Pamene tikulowa chaka chino mawa lino, ndi bwino tisanthule zina mwa nkhani zikuluzikulu komanso magawo amene tidakupatsirani mu Uchikumbe mu 2016.
Ulimi wa ziweto za mbalame Alimi ena adabwekera kuti kuweta zinziri, nkhuku za mazira komanso za Mikolongwe, nkhanga. Alimi adafotokoza momwe ziwetozi zikuwapindulira. Mwa chitsanzo, mlimi wa zinziri adati sizichedwa kukula komanso zimapirira ku matenda. Amene akuweta nkhuku za Mikolongwe adati si zibwerera pamsika komanso kuweta kwake nkosavuta. Kwa alimi a nkhanga, phindu lalikulu ndi lakuti zimaikira mazira ambiri600 pachaka, zomwe si zingatheke ndi ziweto zina za mtunduwu.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Alimi adalimbikitsidwa kupewa matope mmakola awo Malangizo paulimi Kadaulo pankhani yosunga mbewu adalangiza alimi kupewa kusunga chimanga chawo mnkhokwe za nsungwi poopetsa anankafumbwe. Iye adati chimanga chikatha, nankafumbwe amadya nsungwi ndipo mlimi akadzaika chimanga china nankafumbwe amapeza chochecheta. Alangizi enanso adatambasula za kufunika kukolola madzi pamene mvula yagwa komanso kuonetsetsa kuti akupeza mbewu ndi zina zofunikira paulimi nthawi yabwino. Adalangizanso alimi kukhala pagulu kuti asamavutike polandira ulangizi ngakhalenso kupeza misika.
Patsogolo ndi ziweto Alimi a mmadera ena mdziko muno adanenetsa kuti akusimba lokoma ndi ngombe za mkaka pamene adayamba kutsatira malangizo monga kusamalira makola, kufutsa nsipu, kubzala nsenjere, kuteteza matenda ndi zina zotero. Ndipo ena adati iwo koma akalulu amene akuthana ndi mavuto a kusintha kwa nyengo chifukwa chakudya chawo sichisowa. Kwa ena, kuweta nkhumba ndiye tsogolo labwino pomwe alangizi adanenetsa kuti kukhala ndi makola ouma, kudyetsa bwino, ndiye tsogolo lokoma la ulimiwu. Alimi ena adati koma mbuzi ndiye tsogolo labwino chifukwa sizivuta kudyetsa komanso matenda ndi ochepa.
| 4 |
Mpendadzuwa sulira madzi ambiri Mpendadzuwa ndi imodzi mwa mbewu zimene alimi angapindule nazo. HOLYCE KHOLOWA adacheza ndi Maxwell Chimombo wa mmudzi mwa Cedrick kwa Ngwelero ku Zomba amene akulima mbewuyi. Adacheza motere: Kodi mbewu ya mpendadzuwa imalimidwa bwanji? Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Choyamba mlimi amaunga mizere yokula ndi kutalikana ngati ya chimanga. Kachiwiri, mlimi amayenera kukhala ndi mbewu yabwino osati yobwafuka kapena ya matenda kuopera kuti ingavute kumera. Akatero, mlimi azingodikira mvula.
Chimombo kusankha mpendadzuwa kuti akabzale Kodi mpendadzuwa umabzalidwa ndi mvula yake iti? Mpendadzuwa timabzala kawiri wina timabzala limodzi ndi chimanga mvula yoyamba ija ikangogwa pamene wina timabzala pakadutsa mwezi ndi theka chibzalireni mbewu zina zija chifukwa sumafuna madzi ambiri.
Nchifukwa chiyani mpendadzuwa sumafuna madzi ambiri? Mpendadzuwa umene wabzalidwa ndi mvula uja ukamakololedwa wambiri umakhala mphwepwa chifukwa umakhala kuti udamwa madzi ambiri ali mmunda pamene wabzalidwa kachiwiri uja umakhwima mvula ikadukiza zimene zimachititsa kuti nthangala zake zikhale zangwiro zimene sizivuta malonda pa msika.
Mwachitsanzo, mlimi amene wabzala mpendadzuwa ndi mvula yoyamba akhoza kukolola matumba 20 koma akamazapeta akhoza kutsala ndi matumba 14 chifukwa chimachulukitsa matumbawo ndi mphwepwa pamene mlimi amene wabzala kachiwiri akhoza kukololanso matumba 20 koma akapeta mpendadzuwao akhoza kutsala ndi matumba 19 choncho mpendadzuwa wabwinoyu ndi wachiwiri.
Mwachitsanzo, chimanga changa ndinabzala mu November 2016 koma pano ndili pakalikiliki kulima komanso kusankha mbewu chifukwa mpendadzuwa ndibzala kumapeto kwa January uno kapena kumayambiriro kwa February.
Kodi mpendadzuwa mumabzala bwanji? Timabzala motalikana masentimita 75 phando lililonse komanso pa phando pamayenera kubzalidwa nthangala zosaposera ziwiri kuti mpendadzuwa ukule motakasuka bwino komanso kuti usamaphangirane chakudya cha munthaka.
Mbewuyi ikamera imayenera kumasamalidwa bwino makamaka poyipalira mwakathithi kuti mmundamo musakhale tchire limene ndi chiopsezo cha mbewu.
Dothi limene limakhala bwino kulimapo mpendadzuwa ndi lotani? Mpendadzuwa umachita bwino mdothi lililonse koma dothi la makande ndiye pachimake chifukwa limasunga madzi pamene dothi la mchengachenga mbewuyi imabereka mosisitika chifukwa madzi amalowa pansi msanga mnthaka kusiya mbewuyi pamoto.
Kodi mpendadzuwa umagwidanso ndi tizilombo kapena matenda? Mmmmmm pamenepo sindikudziwa bwinobwino chifukwa chiyambireni mpendadzuwa wanga sunagwidwepo ndi matenda. Chinsinsi changa ndi chakuti mmunda mwanga mumakhala mwaukhondo nthawi zonse zimene ndikukhulupirira zimathandiza kupewa matenda ndi tizilombo.
Ndi mavuto anji amene mumakumana nawo pa ulimiwu? Vuto lalikulu ndi misika yodalirika ya mpendadzuwa chifukwa kwathu kuno amatigula mpendadzuwa ndi mavenda. Kuipa kwa mavendawa ndi kwakuti iwowo ndi amene amatipangira mitengo. Nthawi zambiri mavendawa akafika amatiuza kuti malonda a mpendadzuwa sakuyenda bwino kumisika ikuluikulu mtauni choncho atigula pa mitengo yotsika. Ndiye chifukwa ife kumisika ikuluikuluko sitimakudziwa timangogulitsa pa mitengo imene mavendawo afuna.
Mwachitsanzo, mu 2016 alimi timafuna tikumagulitsa pa mtengo wosachepera K200 pa kilogalamu koma mavenda atafika kuno amatigula pa K170 zimene zinatiwawa kwambiri.
Vuto la kusowa kwa misikali mukuganiza lingathe bwanji? Tikupempha eni makampani komanso akuluakulu a zaulimi mdziko muno kuti abwere kwathu kuno adzadzionere okha mmene anthu tikulimira mpendadzuwa chifukwa kwathu kuno tiliko alimi ambiri komanso adzatipatse upangiri wa mmene tingamapezere misika yodalirika ya mpendadzuwa chifukwa mavendawa akutidyera masuku pamutu.
| 4 |
ISAMA Yawopseza Kuti Ichita Ziwonetsero Ngati Sukulu Sizitsekulidwa Akuluakulu a sukulu zoyima pazokha zomwe zili pansi pa bungwe la Independent Schools Association of Malawi (ISAMA) awopseza kuti achita zionetsero ngati mtsogoleri wa dziko lino satsegula sukulu pasanafike pa 5 June chaka chino.
Iwo anena izi pa msonkhano wa atolankhani omwe bungweli linachititsa mu mzinda wa Blantyre.
Malingana ndi mneneli wa bungweli mbusa Hanna Mijoya ati aganiza zochita izi powona kuti ufulu wa ana pa maphunziro ukuphyanyidwa, ndipo ndondomeko zomwe boma layika zophuzilira monga pa makina a intaneti komanso pa wailesi sizikuthandiza ana onse mdziko muno.
Padakalipano misonkhano ya ndale ikuchitika ndipo ana a sukulu akumapita nawo ku misonkhanoko koma chonsecho sukulu ndi zotseka. Ndiye pamenepa kuteteza anako kuli pati, anadabwa motero mayi Mijoya.
Iwo anati ngati mtsogoleri wa dziko linoyu angawayitane kuti akakambirane za nkhaniyi ali okonzeka kutero ponena kuti ngati sizisintha iwo apitilira ndi ganizo lawo lochita ziwonetsero.
| 3 |
General Kanene watuluka mndende Mtsogoleri wa dziko la Zambia Edgar Lungu wakhululukira ndi kulutsa mundende General Kanene, woimba wotchuka mdzikolo, yemwe dzina lake lenileni ndi Clifford Dimba.
Ndi mfulu tsopano: General Kanene Ndipo Lungu walangiza General Kanene kuti akhale kazembe pantchito zolimbana ndi mchitidwe wochita zachisembwere ndi ana ochepa misinkhu mdzikolo.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Malinga nyuzi ya pa Intaneti yak u Zambia yotchedwa Tumfeko.com, General akuti walonjeza Pulezidenti Tembo kuti sadzamukhumudwitsa pantchito yomwe wamupatsa.
Bungwe la azoimbaimba la Zambia Association of Musicians (ZAM) akuti lalandira kumasulidwa kwa Gneral Kanene ndi manja awiri, makamakanso kuti wapatsidwa udindo wa ukazembe kufalitsa uthenga wa kuipa kogwiririra ana kudzera mnyimbo zake.
Chaka chatha, bwalo la milandu lidagamula woyimbayu kuti akagwire ukayidi wa zaka 18 atamupeza wolakwa pamlandu wogwiririra mtsikana wazaka 14.
Iye amasewezera ukayidi wake pa Mukobeko Maximum Security Prison.
Atangokhala kundende kwa miyezi yowerengeka chabe, General Kanene adapeka nyimbo zingapo momwe akufotokoza za mazunzo omwe ankakumana nawo kundendeko.
Iye ankachenjezanso anthu ena kuti asazayerekeze kuphwanya malamulo kuti asakaone zomwe iye wadutsamo.
| 9 |
Zionetsero zaima Anthu zikwizikwi adabwerera manja ali mkhosi kuchoka mmalo a zionetsero Lachitatu pa 28 August 2019 atauzidwa kuti zionetserozo zalephereka kaamba ka chiletso cha khoti la Supreme mumzinda wa Blantyre.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Chitetezo chidali chokhwima Izi ndi zionetsero zomwe a Human Rights Defenders Coalition (HRDC) adakonza kukachitira mmabwalo a ndege komanso mzipata zonse za dziko lino kwa masiku atatu kuyambira Lachitatu mpaka dzulo Lachisanu.
Titaunika mfundo za opempha chiletso, chigamulo nchoti kwa masiku 14 kuyambira Lachitatu pa 28 August, 2019 kusachitike chionetsero cha mtundu uliwonse, panthawiyi, mbali ziwiri ya boma ndi HRDC zikumane nkukambirana momwe anthu angadyerere ufulu wawo wopanga zionetsero komanso pasapezeke munthu wolankhula zomwe zingasokoneze mlandu wa chisankho, chikutero chiletsocho.
Koma pakucha Lachitatu, kudaonetsa kuti ena adasemphana ndi uthengawo chifukwa anthu adayamba kukhamukira mmalo omwe HRDC idalengeza kuti mudzayambira zionetserozo.
Mmawa momwe, apolisi komanso asilikali adali mbwee mmizinda kufuna kuonetsetsa kuti anthu atsatira chigamulo cha khoti la Supreme koma izi sizidakomere anthu ena omwe adakonzekera kuonetsa mkwiyo wawo.
Kodi anthu amenewa bwanji? Chikuwaopsa nchiyani? Bwanji akunjenjemera okhaokha? Akadatisiya tipange zionetsero bwinobwino mesa ndi ufulu wathu? Bomalitu likutiponderedza kwambiri, adatero Mathews Kawinga yemwe amakhala ku Mtandire mumzinda wa Lilongwe.
Pulogalamu ya zionetserozi idagwedeza dziko moti Lachitatu mabizinesi ambiri komanso maofesi ena adali otseka poopa zomwe zakhala zikuchitika pazionetsero zina pomwe anthu ena amatengerapo mwayi nkumathyola maofesi komanso sitolo za anthu nkumaba.
Zionetsero zomwe zikuchitika mdziko muno nzofuna kuchotsa wapampando wa Malawi Electoral Commission (MEC) Jane Ansah chifukwa Amalawi ena akuti sadayendetse bwino chisankho chathachi.
Koma HRDC yatsimikizira Amalawi kuti akatha masiku 14 omwe khothi lapereka, zionetserozo zidzapitilira mopanda mantha aliwonse ngakhale akuopsezedwa.
Mtsogoleri wa dziko lino, Peter Mutharika adalamula apolisi ndi asilikali ankhondo kuti adzagwiritse ntchito mphamvu, zida ndi njira iliyonse kuti zionetsero zisadzachitike.
Mutharika adalankhula izi pamwambo wotsegulira sitima za nkhondo ku Mangochi pa 20 August 2019 koma akadaulo pa ndale ndi malamulo adati Mutharika adalakwitsa chifukwa kuteroko nkuponderedza ufulu wa anthu omwe uli mmalamulo omwe iye adalumbira kuti adzalemekeza.
| 11 |
Bambo Kubalasa Apempha Akhristu AKonde Kuchitira Ena Zabwino Akhristu ampingo wa katolika mdziko muno awapempha kuti azikonda kuchita zinthu zomwe zingawathandize kukhala pafupi ndi Mulungu.
Bambo mthandizi wa Banja Loyera Chilinde parish mu arkidayosizi ya Lilongwe, bambo Maxwell Kubalasa anena izi lamulungu lapitali ku parishiyi pomwenso mpingo wa katolika umachita chaka cha kutsika kwa Mzimu woyera.
Iwo anati zizolowezi zomwe akhristu ambiri amakhala nazo zimakhala zosemphana ndi chifuniro cha Mulungu ndipo anati ngati apempha Mzimu Woyera kuti awatsogolore muzochita zawo, angawathandize koposa pokhala ndi zizolowezi zabwino zomwenso zingakondweletse Mulungu.
Ndi kofunika kuti akhristu azindikire zomwe mzimu woyera amachita mwa munthu amene akugwiramo ntchito. Pali zambiri zomwe anthu akuyenera kupeza akalandira mphatso za mzimu woyerazi maka popititsa patsogolo ntchito yofalitsa uthenga wa Mulungu, anatero bambo Kubalasa.
Akhristu a mpingo wa katolika pa dziko lonse amachita chaka cha Pentecost lomwe ndi lamulungu lotsiliza mu nyengo ya Pasaka.
| 13 |
Mpira wa nkhodzo za pusi mawa ku Sudan Muli kanthu kokakatula ndi sizasi mumzinda wa Omudurman ku Sudan mawali pamene timu ya Big Bullets iphaphalitsane ndi Al Hilal mumpikisano wa CAF.
Iyi mndime yachiwiri yomwe matimuwa afika asadadzabwerezane pa Kamuzu Stadium mumzinda wa Blantyre.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Bullets idanyamuka mdziko muno Lachitatu pabwalo landege la Kamuzu International Airport mumzinda wa Lilongwe ulendo wa ku Sudan.
Kochi wa timuyi Nsanzurwino Ramadhan adatenga osewera 17 paulendowo.
Kochiyo adatenga Vincent Gona ndi Chimwemwe Kumkwawa ngati magoloboyi. Otchinga kumbuyo ndi Sankhani Mkandawire, Miracle Gabeya, Pilirani Zonda, Ian Chinyama, Bashir Maunde ndi Yamikani Fodya.
Osewera pakati adaatenga James Chirapondwa, Fischer Kondowe, Dalitso Sailesi, Victor Limbani, Jaffalie Chande ndi Henry Kabitchi. Kutsogolo kuli Tizgobere Kumwenda ndi Mussa Manyenje.
Timu ya Al Hilal ndi achiyamba kale pokankha chikopa. Bullets siyikuyenera kutengera Al Hilal kumtoso ngati maliro a njoka chifuwa timuyi idafikapo mndime yomaliza ya mpikisanowu mu 1987 ndi 1992.
Timuyi yomwe idakhazikitsidwa mu 1930 mumzinda wa Omudurman, chaka chatha idafika mmasemifainolo a mpikisanowu, akatu ndi ka chisanu kufika mndimeyi.
Iyo yakhalapo akatswiri a ligi ya mdziko la Sudan ya Sudan Premier League Champions ka 27.
Pofuna kuthambitsa Bullets, timuyi idathotha mphunzitsi wake Patrick Aussems wa ku Belgium timuyi itagonja 1-0 ndi KMKM mumpikisanowu.
Al Hilal idapha 2-0 KMKM pakwawo koma koyenda idaphikidwa 1-0. Pano timuyi yalemba mphunzitsi wa ku Serbia, Milutin Micho Sredrojevic amene amaphunzitsa timu ya Uganda.
Zonse zili mawa masana matimuwa asadadzabwerezane pa Kamuzu Stadium. Bullets idatulutsa Club Fomboni ya ku Comoros 3-2.
Bullets isadanyamuke ulendowu, yapuntha Caps United ya ku Zimbabwe 2-1, komanso idatibula Mafco FC 3-0. Awa adali masewero okonzekera mpira wa mawa.
Malinga ndi Ramadhan, kukonzekeraku nkokwanira ndipo akukhulupirira kuti mawa Al Hilal iwona zakuda pakwawo.
Tidali ndi mavuto angapo pamasewero amene tidali nawo ndi Fomboni, koma takonza ndipo nokha mwawona momwe tachitira mmasewero amene tasewera posachedwapa, adatero Ramadhan ponyamuka mdziko muno.
| 16 |
Ana Atetezedwe Ku Gozi Zogwa Mwadzidzidzi-Social Welfare Wolemba: Sylvester Kasitomu Ofesi yoona za chisamaliro cha wanthu ya Social Welfare mboma la Zomba yapempha anthu kuti adzichilimika pothandiza kutetedza ana pa nthawi ya ngozi zogwa mwadzidzidzi.
Mkulu wa kuofesiyi a Stephano Joseph anena izi loweruka pa 31 August pa sukulu ya Primary ya Sunuzi mbomalo pomwe bungwe la Future Vision International limachititsa mwambo wokumbukira Mwana Wa Mu Africa.
A Joseph omwe anafika ngati mlendo wolemekedzeka pa mwambowu adathokodza bungwe la Future Vision International chifukwa chowonetsa chidwi pa ntchito zokumbukira tsikuli.
Lero mmene tabwera ndi mwai wa anthu nawonso apeze nawo mwai wa maphunziro amene angasamalire ana aangono ndi aakulu omwe anakhudzidwa ndi matenda ogwa mwadzidzidzi, antero Joseph.
Pothirirapo ndemanga mkulu wa bungwe la Future Vision International mdziko muno a Newton Sande Sindo apempha anthu a mdera la Sunuzi mboma la Zomba kuti agwiritse bwino uthenga womwe alandira wokhudza mwambo wa tsiku lokumbukira mwana wa mu Africa.
Ngozi ndi chinthu chomwe chimabwera modzidzimutsa ndipo mwazina zimakhudza anhtu olumala komanso ana nde tinachiona cha nzeru kuti tibere kuno tidzapereke uthengawu, anatero a Sindo.
Mdera la Sinuzi mboma la Zomba ndi limodzi mwa madera mbomali omwe amakhudzidwa ndi ngozi zogwa mwadzidzidzi.
| 14 |
Nankhumwa Walimbikitsa Otsatira DPP Akhale a Mtendere Wachiwiri kwa president wa chipani cha Democratic Progressive (DPP) mchigawo cha kumwera Kondwani Nankhumwa wapempha otsatira a chipanichi kuti alimbikitse bata ndi mtendere pamene ntchito yokopa anthu ikupitilira.
Nankhumwa: Mutharika anawina kale chisankho Nankhumwa anayankhula izi pa msonkhano omwe anachititsa ku Ndirande mu mzinda wa Blantyre. Iye ati chipani chawo chimakhulupilira kufotokozera anthu mfundo za chitukuko komanso njira zomwe zingatukule miyoyo ya anthu.
Chisankho tinapanga bwino bwino chaka chatha ndipo owina anawina ndipo Peter Mutharika anawina ndi mavoti ambiri ndipo khoti linagamula kuti Peter Mutharika sangachotsedwe pa mpando koma kuponyedweso voti, anatero a Nankhumwa.
Iwo apempha atsogoleri a zipani zina kuti azikamba Mfundo zokopera anthu mwamtendere osaliti kulimbikitsa ziwawa.
| 11 |
Abwenzi a Radio Maria Apereka Katundu Kwa Ana Osaona, Osamva Abwenzi a Radio Maria mu akidayosizi ya Blantyre alimbikitsa akhristu komanso anthu mdziko muno kuti azitengapo mbali pothandiza anthu 24w, https://www.radiomaria.mw/wp-content/uploads/2019/12/ngomba-768x576.jpg 768w, https://www.radiomaria.mw/wp-content/uploads/2019/12/ngomba.jpg 1040w" sizes="(max-width: 492px) 100vw, 492px" />Ngomba kupereka wina mwa katunduyo Wapampando wa gululi a James Ngomba ndi omwe amayankhula izi pomwe anayendera ndi kukacheza ndi ana omwe ali ndi vuto losaona komanso kumva pa sukulu za Montfort Demonstrations school for the deaf komanso Mary view school for the blind ku Nguludi mu mzinda wa Blantyre lamulungu pa 1 December 2019.
A Ngomba anati anachiona chanzeru kuti athandize ana wa ngati njira imodzi yogwira ntchito za chifundo.
Ndife okhutira kuti tinabwera kudzacheza komanso kuthandiza ana omwe amasowa thandizo ndipo taona kuti akusowa zambiri choncho tikonzanso ulendo wina kuti tibwerenso kudzawathandizaanatero a Ngomba.
A Ngomba anati ndi udindo wa munthu aliyense amene ali ndi kuthekera kuthandiza anthu omwe ndi osowa makamaka ana akuno omwe ali ndi vuto losaona komanso kumva.
Poyankhulapo mmawu ake mphunzitsi wamkulu pa Mary view schools for the blind a James Khuku anathokoza gululi kamba kowapatsa katundu yemwe ati wafika mu nthawi yoyenera pomwe iwo akukumana ndi mavuto akusowa kwa chakudya.
Katundu yemwe talandira lero atithandiza kwambiri kuchepetsa mavuto a zakudya omwe alipo pa sukulu pano.anatero a James Khuku.
Apa a Khuku apempha anthu akufuna kwabwino kuti awathandize kamba koti pa sukulupa amakumana ndi mavuto osiyanasiyana makamaka pa nkhani ya zakudya.
Wina mwa katundu yemwe gululi lapereka ndi monga ufa,mpunga, nyemba ndi mafuta ophikira ndipo ndi za ndalama zokwana 200 thousand kwacha.
| 14 |
Asemphana maganizo pa zoletsa masacheti Pali kusemphana maganizo kutsatira kulengeza kwa boma kuti laletsa mowa wa mmasacheti umene Amalawi ena akhala akuthudzulira.
Pamene mafumu ena akugwirizana ndi ganizoli, ena akuti palakwika ndipo boma libweze moto.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Msonkhano wa nduna pa 16 February udavomereza zoletsa mowawu.
Kuletsaku kumatsatira chigamulo cha bwalo la milandu lomwe lidati nthambi yoona kuti katundu wopangidwa mdziko muno akukhala wa pamwamba la Malawi Bureau of Standards siyilidalakwe kuletsa makampani wotcheza mowawo kuleka kutero.
Nkhaniyi pano yabwerera kukhoti pamene makampani amene amafulula mowawu atengera nkhaniyi kubwalo lalikulu kusaka chigamulo china.
Kulengeza kwa bomaku kudadzetsa mpungwepungweena akudana ndi lingaliroli, pomwe ena akugwirizana nalo.
Mwachitsanzo, msabatayi mkulu amene wakhala akumenya nkhondo yoletsa mowawu, Jefferson Milanzi, wa bungwe la Young Achievers for Development (YAD), adafuna kupandidwa ndi anyamata ena ku Zingwangwa mumzinda wa Blantyre polimbikira kuti mowawu uletsedweretu.
Adalipo anthu pafupifupi 15 omwe amati ndinene chifukwa chimene mowawu wandilakwira. Adati athana nane chifukwa cholimbikitsa nkhondo yoletsa mowawu, adatero Milanzi amene akuti adathamangira kupolisi ya Soche mumzindawu kukadandaula.
Nawonso mafumu ena adauza Tamvani msabatayi kuti palakwika kuletsa mowawu chifukwa achinyamata amapezerapo phindu pogulitsa mowawu.
Senior Chief Nthache mboma la Mwanza akuti achinyamata ambiri mmidzimu akhala akupha makwacha ochuluka pogulitsa mowa wa mmasachetiwu.
[Zoletsa mowa wa mmasachetizi] ndiye ziwonjezera umphawi wathu wakalewu. Ndiye achinyamata azitani? Ngatitu kuli bizinesi yomwe imawapatsa ndalama zochuluka achinyamata kumudzi kuno ndiye ndi mowawu, adatero Nthache pouza Tamvani.
Nthache adati si mowa wokha wa mmasacheti umasokoneza achinyamata kotero sakuona chifukwa choletsera.
Kuli mowa wa kachasu womwenso ndi mowa woipa kwambiri. Kuli mtonjani komanso ena amasuta chamba. Ndiye si masacheti okha amene ali ndi vuto. Boma liganizepo bwino pamenepa, adatero Nthache, amene adati samwa mowawu.
T/A Mwakaboko wa mboma la Karonga nayenso adagwirizana ndi Nthache pamene adati anthu kumeneko akukatamuka ndi bizinesi ya mowa wa mmasacheti.
Koma Mwakaboko akugwirizana ndi ganizo logulitsira mowawu mmabotolo kulekana ndi kuletseratu kutcheza mowa wotere chifukwa akuti zikhudza bizinesi ya anthu ambiri kumudzi.
Koma T/A Kabunduli wa ku Nkhata Bay akugwirizana ndi ganizo la boma loletsa masacheti ponena kuti achinyama ambiri asokonekera ndi chakumwa chaukalichi.
Achita bwino, ambiri akufa komanso kusokonekera chifukwa cha masacheti. Koma aiwalatu kuletsanso mabotolo a pulasitiki. Amenewonso aletse kuti mowawu usaonekenso, adatero Kabunduli.
Pali chiopsezo chachikulu kuti makampani ambiri amene amapanga mowawu angathe kutseka chifukwa cha phindu lochuluka lomwe amapeza akagulitsa mowawu.
Pamene makampaniwa akutseka, bomanso litaya ndalama zankhaninkhani zomwe limapeza makampaniwa akakhoma msonkho.
Koma mneneri wa boma, Kondwani Nankhumwa, adauza atolankhani sabata yatha kuti maso a boma ali posamala miyoyo yambiri yomwe ikusokonekera ndi mowawu, osati phindu lomwe boma likupeza.
Mneneri mu unduna wa zaumoyo Henry Chimbali adati nkhaniyi ikukhudzanso unduna wawo chifukwa mowawu umakhala ndi mavuto ena amene umabweretsa ngati munthu wamwa.
Chimbali akuti mowawu umachititsa kuti chiwindi chilephere kugwira bwino ntchito yake komanso umayambitsa matenda a shuga (diabetes).
Si mavuto okhawa, mowawu umayambitsa mitundumitundu ya matenda a khansa komanso ena okhudza ubongo, adatero Chimbali amene adati mdziko muno anthu 8 pa 100 aliwonse osaposa zaka 25 amamwa mowawu.
Mabungwe ena akhala akunena kuti ndibwino boma lipeze ndondomeko zothana ndi kumwa mowa moposera muyezo wake.
Mu 2012, dziko la Zambia lidaletseratu mowawu ndipo lidalanda zitupa za makampani amene amafulula mowawu komanso kubweretsa mowawu mdziko lawo. Yemwe adali nduna ya zamaboma angono pa nthawiyo, Nkandu Luo adati boma lidabwera ndi ganizolo chifukwa cha zotsatira zoipa zomwe mowawu udabweretsa mdzikomo.
Ndunayo idati ganizolo lidadzanso boma litafunsa mbali zonse za dzikolo. Mowawu mdzikolo umatchedwa kuti Tujilijili pamene mdziko muno timangoti masacheti. Ndunayo idati munthu amene apezeke akugulitsa kapena kufulula mowawu adzaseweza kundende kwa zaka ziwiri.
| 7 |
Chithunzithunzi cha gogo wathu Mukunyasitsa nkhope mwayambana ndi ndani Munthu wokwiya saoneka bwino Amakhala ngati mtembvo omwe ukanka kumanda Maliro ake ochita kupha ndi mwala Chisale watuluka nkumangidwanso Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Iyi ndi nyimbo ya Phungu Joseph Nkasa imene inkaphulika malo aja timakonda pa Wenela tsiku limenelo.
Kuchipululu Kalekalelo, anasankha wolakwika Waumphawi, ndi umbuli Anasankha wolakwika Koma Gervazzio! Sindidziwa kuti amaganiza chiyani posankha nyimbo.
Posakhalitsa idatulukira basi. Adatulukamo Moya Pete, tsinya lili kuno! Mumandinena kwambiri, kuti ndinatenga mbuzi 200 kupita kukaonana ndi Bani Kimwezi wa Nations Unie. Nonsense! Nonsense! Mulibe nzeru nonse, kodi simudziwa ndili nawo ochuluka makobidi? Kafunseni mabanki a ku Switzerland! Izi ndi zangazanga ndalama. Nkati ndikuuzeni, pamwezi ndimalandira K1 400 ndiye mukati ndimayenda kuti ndizidya ndalama zanu. Nonsense! adatero tisanamupatse moni.
Pomwepo, adayamba kukwapula basiyo mokwiya.
Nonsense kwambiri. Sindidya pakhomo panu. Ndikapita ndi mbuzi 601 dziko lija la Amerigo Vesipusi mwati ndalakwa? Kodi enatu anabwera masauzande! adazaza Moya Pete.
Inetu ndimadabwa kuti munthu akangolawa zamchere ndithu amapenga ngati mbuzi! Abiti Patuma amaganizanso chimodzimodzi.
Akulu, khazikitsani mtima pansi. Sikuti mukamalankhula ndi mkwiyo ndiye kuti mukunena zoona. Ndipo enafe timaona kuti munthu akamakalipa, kutenga aliyense ngati chidzukulu chake, timadziwa kuti pali chimene akubisa. Timakumbukatu za Adona Hilida, Mpando Wamkulu ngakhalenso uyu mwati ndani uyu. Mfumu Mose, adatero Abiti Patuma.
Abale anzanga, chiwanda choyenda ndi mapazi ichi.
Ndakwiya kwambiri. Ndikhozanso kuzisiya kwambiri! Kodi mwaiwala kuti gogo uja naye ankakwera ndege monga enanu muchitira kabaza? Bwanji simunkamutsutsa? Ine ndikangoti ndilaweko kabaza wa ndegeyu mwati mfwemfwemfwe! Nonsense! adatero Moya Pete, uku akunyamula tambula ya madzi ozizira.
Adamwa. Adanyambitira. Adatafunira ngati mmadzimo mudali nsenga.
Gogo amanenedwa apatu ndi uja adandipeza ndikulima osavala ndili kwathu kwa Kanduku. Inde, gogo yemwe uja adapita uku ndi uko kukanena kuti adandipeza ndili buno bwamuswe! Mwaiwalatu china chake akulu. Gogo mukunenayo ulamuliro wake udali wayekhayekha ndipo padalibe omutsutsa. Ifetu tikamakutsutsani timakufunirani zabwino, adatero Gervazzio.
Ana osakhwima paliombo. Mwaiwala kale zazikulu zimene ndakuchitirani? Munali yani, anthu oipa mwapanga bwanji? adafunsa Moya Pete.
Palibe adayankha. Aliyense adafa nalo phwete.
Tsoka lake, mukakhala kuchipinda kwanuko, kudikira kumwa wamkaka tiyi mumaona ngati zonse zikuyenda. Kodi inuyo a Dizilo Petulo Palibe mudawauza anthu kuti mudzathana ndi zoti tizichita Jump Carefully? Nanga zolipira kundagala mudanenapo? Taipa lero? adatero Abiti Patuma.
Abale anzanga, palibe icho ndidatolapo.
| 15 |
Ndege ya ufiti ikodwa ku Kasungu Ngakhale malamulo a dziko lino amakana kumutchula munthu kuti ndi mfiti, Amalawi ambiri amakhulupirira kuti ufitu uliko.
Anthu a mmudzi mwa Gundani mboma la Kasungu adodoma ataona chinthu chooneka ngati ndege chomwe akuchiganizira kuti ndi ndege ya afiti chitagwa mmudzimo.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Msangulutso utafufuza chomwe chidachitikita, udapeza kuti ndegeyo idagawa pakhomo pa Yusufu Abubaka Ali yemwe akukhulupilira kuti akola mfiti zomwe zakhala zikusautsa banja lawo.
Anthu amenewa adalodza akazi anga koma ndi mmene agwidwiramu akazi anga akhala bwino, adatero Ali.
Mkazi wa bamboyo Liness Kaulongo wakhala akudwala kwa nthawi yaitali ndipo kuchipatala cha boma ku Kasunguko adawauza akayesere zachikuda.
Tidapita kwa asinganga komwe adationetsa anthu anayi kuti ndi omwe akusautsa banja lathu. Singangayo adatipatsa mankhwala omwe adati tikaike panyumba yathu kuti ndidzakole mfiti zomwe zimanditambilazo, adatero Ali.
Iye adati sanadabwe kwambiri mkazi wake akuuza kuti kunja kwa nyumba yawo kwagwa chinthu chooneka ngati ndege.
Kaulongo, adati adadabwa kuona chinthu chamaonekadwe ngati ndege chili panja panyumba yayo pomwe adatuluka usiku kukataya madzi.
Mneneri wapolisi mboma la Kasungu Edwin Kaunda adatsimikiza kuti iwo akusungadi chinthu chomwe chikuganiziridwa kuti ndi ndege yaufiti.
Iye adati adapita pamalopo kukakhazikitsa bata chifukwa chinthucho chinkabweretsa mpungwepungwe pa malopo.
Ife tidapita kukatenga chinthucho ndipo tili nacho kuno kupolisi, adatero Kaunda.
| 19 |
Chipongwe mmaofesi mwinamu Pali maofesi angapo, maka a boma, omwe amachuluka chipongwe kaya titi mwano polankhula ndi anthu ofuna chithandizo.
Ofesi ngati za Immigration, Road Traffic, komanso mzipatala, kumakhala anthu oti akamakulankhula amachita ngati kuti ndiwe wosazindikira.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ukafika pakauntala, amakufunsa tikuthandizeni? akuyangana kumbali kapena ngati akukuyangana amakuthira diso loderera kapena lotopa nawe.
Anthu ambiri ogwira ntchito mmalowa amakhala ngati adatopa kalekale. Ukapita kufuna chithandizo ukhoza kuyesa ngati mwayambana. Kulankhula ndi munthu wamkulu ngati akuyankhula ndi mwana.
Nthawi zina kuchipatala akakufotokozera ndondomeko ya kamwedwe ka mankhwala ndiye ukapandakumva bwino umachita kulephera kufunsa kuti afotokozenso kuopa kuzaziridwa.
Ukamafotokoza zowawa mthupi, usanamalize nkomwe olemba mwankhwala walemba kale. Amachita ngati ukumutayitsa nthawi.
Kukakhala ku Immigration, chipongwe chimayambira ndi mlonda wa pakhomo. Kulankhula ndi anthu mwachipongwe chokweza ngati ukudzapempha pakhomo pake.
Ukalowa mkatimo ndiye mumakhala chidodo cha dzaoneni. Chiimire pamzere mumangomva za mavuto osatha a network.
Ukafika pamalo oti ujambulitse chithuzi kaya chala, anthu ogwira ntchito ambiri amangoyankhula mwamgwazo, moderera ndi mokalipa.
Mabwana kumaofesi ndatchulawa komanso maofesi ena a boma, mutaunika kagwiridwe ka anthu anu antchito, maka awo amakumana ndi anthu, kuti mutithandize izi zichepe.
Phasipoti kaya laisensi ikatha, umachita kuda nkhawa kuti ukapezekenso mmaofesi amenewa.
| 15 |
Bambo Wanjatidwa Atapezeka Ndi 300 Kilogram Ya Chamba Apolisi mboma la Mangochi akusunga mchitokosi bambo wina wa zaka 49 kamba kopezeka ndi chamba opanda chilolezo.
Mkuluyo akuti amalima mbewuyi Malinga ndi mneneri wa apolisi mbomalo Inspector Rodrick Maida, munthu wina wakufuna kwabwino anadziwitsa apolisiwa kuti bamboyu Mariyo Makweche amapezeka ndi chamba ndipo apolisiwa atakachita chipikisheni anamupeza mkuluyu ndi chamba chokwanira makilogram 300.
Maida wati akuganiza kuti mkuluyu amalima chambachi kumudzi kwawo ndipo wati padakalipano chambachi achitengera ku Bvumbwe Research Station kuti akachipime.
Mariyo akuyembekezeka kukawonekera ku bwalo la milandu kuti akayankhepo pa nkhaniyi ndipo apolisi mbomali ayamikira ubale wabwino omwe ulipo pakati pa iwo ndi anthu a mderali.
| 14 |
Ntchito yasowa, wayamba ulimi wa kabichi Adabwera mtauni ya Blantyre kudzasaka ntchito atamaliza Fomu 4. Adaponda paliponse kukasaka ntchito, makalata chilembelenicho ndi satifiketi yake ya Malawi School Certificate of Education (MSCE) koma palibe amene adamutenga. Yankho lidali lobwerera kumudzi kuti akangoyamba ulimi. Lero ulimi wa kabichi wayamba kumupatsa ndalama, wagula ngombe ziwiri, njinga, nkhuku komanso wamangitsa nyumba. Iyi ndiyo nkhani ya Patrick Khuliwa, yemwe akucheza ndi BOBBY KABANGO.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Kodi tingachezeko, wawa? Kwambiri, palibe choletsa. Kaya mufuna ticheze nkhani zanji potitu tangokumana kumunda kuno.
Mbiri yanu komanso ulimi wa kabichi Vuto palibe, uwu ndi munda wanga, ndalima ndekha ndiye palibe pamene pangandivute kufotokoza.
Khuliwa akuti watola chikwama muulimi wa kabichi Koma mbiri yanu ndi yotani? Ndimachokera mmudzi mwa Mulunguzi kwa T/A Juma mboma la Mulanje. Ndili ndi satifiketi ya Fomu 4 yomwe ndidapeza mu 2007. Nditakhoza, ndidapita ku Blantyre monga ambiri amachitira komwe ndimakasaka maganyu. Achimwene, ndidavutika osati masewera, ntchito zikusowa. Zoti ndakhoza mayeso a Fomu 4 ngati bodza, ena ake amati mwina ndiyese ntchito za mnyumba koma malipiro ake adali ochepa. Mapeto ake ndidabwerera nkudzayamba ulimi wa kabichi.
Ulimiwu mudayamba liti? Mu 2007 momwemo nditabwerako kutauni.
Chaka chino mwalima munda wokula bwanji? Nanga mukupeza zotani? Ndalima theka la ekala. Munda umenewu chaka chino ndakolola matumba 20 a kabichi olemera makilogalamu 100 lililonse.
Mwapha ndalama zingati? Thumba limodzi ndimagulitsa K9 000, pamatumba 20 ndidapeza K180 000 koma kabichi wina ndimagulitsira kumunda konkuno.
Msika mumaupeza bwanji? Panopa palibenso nthawi yokayangana msika chifukwa mavenda akumadzagula kumunda konkuno koma chomwe tikuonetsetsa nchakuti mtengo uzikhala wabwino. Monga poyamba timagulitsa K7 000 pa thumba limodzi koma pano lachita kukwera.
Pa chaka mukumalima kangati? Nthawi ya mvula ndimalima kamodzi, koma mvula ikangotha ndimalima kabichi wamthirira yemwe ndikumalima kawiri, kusonyeza kuti ndikumalima katatu.
Uyu ali mmundayu ndi wachingati? Wachiwiri. Ndayambanso kukolola moti sabata ino ndikumaliza kukolola ndipo ndayamba kale kulima wina. Kutereku mbali inayo ndabzala kale. Pofika December ndikhala ndikukolola kusonyeza kuti ndidzakhala ndikukonzekera ulimi wa mvula.
Ulimi woyamba ndi wachiwiriwu mwapeza ndalama zingati? Kupatula zochotsachotsa, ndalama yogwirika yomwe ndidaisunga idalipo K250 000. Ndalama zinazo ndimagwiritsira ntchito pakhomo.
Chiyambireni ulimiwu mwapangapo chiyani? Ndamangitsa nyumba ya njerwa zootcha yomwenso ndi yamalata; ndagula ngombe ziwiri ndipo ndikulankhula pano zili mkhola mwake; komanso ndili ndi nkhuku ndi njinga. Ntchito zapakhomo zikuyenda kuchokera mkabichi yemweyu.
| 2 |
Apolisi, mabungwe akufuna kuteteza ufulu wa ana Apolisi ati agwirana manja ndi mabungwe osiyanasiyana pa ntchito yoteteza ufulu wa ana mdziko muno.
Mkulu wa polisi ya Chirimba, Aubrey Chimenya ndiye adalankhula izi pamsonkhano womwe bungwe la Chisomo Childrens Club idachititsa pa sukulu ya Chirimba mu mzinda wa Blantyre.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mwana ali ndi ufulu wophunzira, koma nzokhumudwitsa kuti mmalo motumiza ana kusukulu makolo akumatumiza ana awo kukagulitsa zibwente, zitumbuwa, zindasi, madonasi ndi zinthu zina, adatero Chimenya.
Iye adati agwira ntchito ndi mabungwe osiyanasiyana kuphatikizirapo la Chisomo kuti athane ndi mchitidwewu.
Tiziyenda mmisika ndipo tikapeza ana akugulitsa katundu mmisika tiziwaitana kuti atiuze zolinga zawo, adatero Chimenya.
Mkulu wa bungwe la Chisomo mchigawo cha kummwera, Auspicious Ndamuwa, adati cholinga cha bungwe lake ndi kuonetsetsa kuti ufulu wa ana ukutetezedwa.
Iye adati mwana ali ndi ufulu wopatsidwa dzina, mankhwala akadwala, kutetezedwa, kusingiridwa chinsinsi, wosonkhana ndi a mnzake, wolankhula zakukhosi ndi maphunziro.
Ntchito yopeza ndalama zogwiritsira pakhomo si ya ana, koma makolo. Choncho makolo asaphwanye ufulu wa maphunziro wa ana powatumiza kukagulitsa malonda anzawo ali mkalasi, adatero Ndamuwa.
Mphunzitsi wamkulu wa pa sukulupo, ndi yemwe adaimirira nyakwawa ya mderalo adavomereza kuti ana ambiri amapezeka pa msika wa Chirimba nthawi ya maphunziro.
| 7 |
Chimodzi Jnr career stalls Former Silver Strikers captain and Flames midfielder Young Chimodzi Jnrs career has stalled as he is yet to depart for India where he, in March, signed for Kenkre Sports Club.
Two affiliates cry foul over Covid-19 relief package No hard feelings, says Nyamilandu Chisale watuluka nkumangidwanso The holding midfielder yesterday explained that he was waiting for his foreign-based agent to arrange with Kenkre for his air ticket.
Chimodzi (L) : I miss the game The delays have also cost Chimodzi his Flames career. He signed a year-long contract with the India League division two side.
The visa is out but my agent, who also manages Tawonga, is very busy. I miss the game but it is a matter of being patient, he said yesterday.
He is now four months into his contract and he insisted that he would decide later in the event of further delays.
Kenkre chief executive officer Joshua Lewis assured to meet all expenses during his stay in India, according to an earlier story published in March by The Daily Times.
This is to inform you Mr Young Lawrence Chimodzi; a professional football player hailing from the Republic of Malawi is currently representing our club, Kenkre FC. The club will also bear all expenses during his stay in India, reads part of the letter.
| 16 |
Makhansala Awiri a Khonsolo ya Ntcheu Alowa UTM Mtsogoleri wa chipani cha UTM yemwenso ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr. Saulos Chilima wapempha anthu a mboma la Ntcheu kuti adzavotere mgwirizano wa Tonse Alliance kuti dziko lino lipite patsogolo.
Dr. Chilima omwe akuzayimira ngati wachiwiri kwa Dr. Lazarus Chakwera pa chisankho chomwe chikubwerachi amayankhula izi paulendo wawo woyimayima omwe amachititsa lachisanu mboma la Ntcheu.
Chilima kutsindika mfundo pa umodzi mwa misonkhano yomwe anachititsa Iwo awuza anthu kuti iwo pamodzi ndi anzawo agwirizana kuti adzakhazikitse thumba la ndalama zokwana75 billion yomwe cholinga chake chidzakhala kuthandiza anthu mmaboma onse kupeza ngongole zopangira mabusiness osiyanasiyana.
Boma lililonse lizapatsidwa 1 billion ngati thuma lothandiza anthu ozungulira bomalo kutennga ngongole, anatero Dr. Chilima.
Iwo atinso azamalizitsa bwalo la zamasewero komanso nsewu wa Tsangano-Mwanza zomwe zinayima, komanso kusitsa fetereza ndi kupereka malipiro kwa athu oyambira zaka 65 kupita mtsogolo.
| 11 |
Apempha anthu kupanga manyowa Sukulu ya aphunzitsi Development Aid from People to People (Dapp) Chilangoma ku Blantyre yapempha anthu kupanga manyowa kuti akhale ndi mbewu zathanzi komanso zochuluka.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mkulu wa mapologalamu pasukuluyo, Hope Funsani, adanena izi Lachiwiri pamwambo wopereka chimbudzi chamakono mdongosolo la School Garden and Nutrition (SGN) pa sukulu ya pulaimale ya Samama mmudzi mwa Kamowa kwa T/A Kuntaja mbomali.
Chimbudzicho, skyloo, chimalimbikitsa ukhondo ndi kupereka danga lopanga manyowa kuchoka ku ndowe za anthu.
Chimbuzi cha skyloo pa pulayimale sukulu ya Samama Funsani adati manyowa amathandiza mbewu kupirira ku chiwawu chifukwa amasunga chinyotho kwa nthawi yaitali.
Feteleza amaonongetsa ndalama, sabwezeretsa chajira mnthaka ndipo timafunika kuthira chaka chilichonse. Manyowa amathandiza mbewu kukhala zathanzi, zochuluka ndipo umathira mmene wafunira. Banja lililonse likhalenso ndi polima ndiwo za masamba, iye adatero.
Pothirira ndemanga pa chimbuzichi, mkuluyu adati chithandiza anthu kupanga manyowa ochuluka chifukwa azipeza ndowe zawo zomwe osati za ziweto zokha.
Mfumu Kamowa idayamikira Dapp kaamba ka chimbuzicho, koma idapempha thandizo ndi upangiri omangira zambiri kuti anthu apindule.
Tadziwa kuti manyowa atithandiza kuthana ndi njala ikudza kaamba ka kusintha kwa nyengo. Ndilimbikitsa anthu kuchigwiritsa ntchito kuti tiyambe kusunga manyowa. Koma tithandizeni pomanga zambiri kuti banja lililonse lizisunga chinyontho chake, adatero Kamowa.
Mphunzitsi wamkulu pasukulu ya Samama, Lameck Senzani, adati aonetsetsa kuti anthu akugwiritsa ntchito chimbuzicho moyenera kuti chiwapindulire.
| 4 |
Tidziwane ndi Enock Balakasi wa Joy Radio Atolankhani mdziko muno amakumana ndi zokhoma zambiri makamaka pofuna zoti auze mtundu wa Amalawi. Mwa zifukwa zina, kusoweka kwa lamulo lothandiza kuti atolankhaniwa azitha kutola nkhani paliponse popanda chowapinga ndi nkhani yomwe pakalipano ili mkamwamkamwa. STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi Enock Balakasi wa kanema ndi wayilesi ya Joy pankhaniyi.
Balakasi: Ufulu wolemba uli papepala basi Dzina lako ndani mbale? Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Dzina langa ndi Enock Balakasi, wachiwiri mbanja la ana 7. Ndimachokera mmudzi mwa Matandika kwa T/A Nkula mboma la Machinga. Pano ndimayanganira ofesi ya Lilongwe ya kanema ndi wayilesi ya Joy koma ndidalembedwa ntchito ngati mkonzi ndi mtolankhani.
Udayamba liti za utolankhani? Utolankhani ndidauyamba mu 2007 nditamaliza maphunziro anga kusukulu yophunzitsa ntchito ya Blantyre Business College. Yemwe adandilimbikitsa kuti nditsatire za utolankhani ndi malume anga a Dr Rodrick Mulonya ndipo pano ndikupitirizabe maphunziro a zautolankhani chifukwa sindidafike pomwe ndimafuna.
Zimaonekatu ngati atolankhani mdziko muno amavutika kuti apeze nkhani, kodi vuto nchiyani? Choyamba ndivomereze kuti ufulu wolankhula ndi kulemba ulipo koma kandodo kokwapulira kamakhala mkhundu. Ufuluwu umaoneka kuti uli papepala basi koma kuti ukwaniritsidwe pamavuta. Mwachitsanzo chabe, atolankhani akhala akugubuduka kupempha kuti pakhale lamulo lowapatsa mphamvu zogogoda khomo lililonse kukatola nkhani, lija amati Access to Information (ATI) koma zikuoneka kuti akuluakulu ena ali ndi maganizo ena pankhani imeneyi. Lamuloli litangotheka, zonse zikhoza kusintha nkumayenda bwino pantchito ya utolankhani.
Nkani ina ndiyakuti nthawi zambiri mdziko muno pamatenga nthawi kuti chomwe chachitika chimveke monga momwe maiko a anzathu amachitira, pamenepanso ndi nkhani ya lamulo lomweli? Mbali ina tikhoza kunena kuti lamuloli limatengapo gawo lake koma kwakukulu ndi kusowa kwa zipangizo. Nyumba zambiri zoulutsa ndi kusindikiza nkhani muno mu Malawi zilibe zipangizo zokwanira ngati momwe makampani akunja mukunenawo. Mwachitsanzo, kuno kwathu pakakhala zochitika, nthawi zambiri timadalira omwe akonza zochitikazo kuti anyamule atolankhani komwe kuli kulakwitsa chifukwa pamenepo mumakhala kuti mwayamba kale kugwa mbali ya okutenganiwo. Njira yabwino ikadakhala yoti makampani oulutsa ndi kusindikiza nkhani akhale ndi zipangizo zawozawo kuti akafuna kukatola nkhani asamakhale ndi mbali ina iliyonse.
| 15 |
Chilima akhazikitsa UTM ku Blantyre Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Saulos Chilima, mawa akhazikitsa gulu la United Transformation Movement (UTM) ku Njamba mu mzinda wa Blantyre.
Polankhula ndi Tamvani, mneneri wa gululi, Joseph Chidanti Malunga, adati chilichonse chokonzekera kukhazikitsidwaku chili mchimake.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Chilima kukhazikitsa UTM pa bwalo la Masintha ku Lilongwe Tili ndi masomphenya a aakulu omwe amangiririka pa ndondomeko 12 zosinthira dziko lino. Anthu aku Lilongwe alawa kale zina mwa zinthu zomwe tikufuna kuchita, adatero Malunga.
Msonkhanowu udayenera kukachitikira pa bwalo la sukulu ya Nyambadwe, koma Malunga adati asintha kaamba koti bwalolo ndi lalingono.
Wapampando wa gululi, Noel Masangwi, adati ukatha msonkhano wa ku Blantyre, akakhazikitsanso gululo mchigawo cha kumpoto.
Sabata yatha UTM idakhazikitsidwa pa bwalo la Masintha mu mzinda wa Lilongwe ndi chinantindi cha anthu chidafika pamwambowo.
Ena mwa anthu omwe adafika ndi Sipika wa Nyumba ya Malamulo, Richard Msowoya, akazi a atsogoleri akale a dziko lino, Callista Mutharika ndi Patricia Shanil Dzimbiri, phungu wa mboma la Balaka, Lucius Banda, aphungu a DPP a mboma la Mulanje, Bon Kalindo ndi Patricia Kaliati.
UTM idayambika Callista atapempha mtsogoleri wa dziko lino, Peter Mutharika, kuti apereke mwayi kwa Chilima kuti adzaimire DPP pa zisankho za chaka cha mawa.
Mutharika adakana pempholo zomwe zidachititsa kuti Chilima ndi anthu ena atuluke mchipanicho nkuyambitsa gulu la UTM.
| 11 |
Kutambasula nthenda ya kadzamkodzo Kunjaku kuli nthenda zosiyanasiyana koma nthenda zina ukamva, kudulitsa mutu wazizwa. Sabata yapitayi, nduna ya zaumoyo, Dr Peter Kumpalume, adatsogolera Amalawi kutsegulira nyengo yokumbukira matenda a kadzamkodzo (Fistula) mboma la Kasungu. STEVEN PEMBAMOYO adachita chidwi ndi nthendayi ndipo adacheza ndi ndunayi, yomweso idagwiraponso ntchito ya udokotala, kuti itambasule za nthendayi motere: Kumpalume kutsindika za vuto la kadzamkodzo Anduna, anthu akudziweni.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Ndine Dr Peter Kumpalume, nduna ya zaumoyo, komanso phungu wa chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) kudera la kumadzulo kwa boma la Blantyre. Ndagwirapo ntchito zachipatala mmadipatimenti osiyabnasiyana mdziko muno ndi maiko akunja.
Kodi apa mukuti pakuchitika zokhudza kadzamkodzo, chimenechi nchiyani? Iyi ndi nthenda yoopsa kwambiri koma anthu ambiri sazindikira. Nthenda imeneyi imagwira amayi ndipo mzimayi akagwidwa ndi nthenda imeneyi, moyo wake umasinthiratu. Amadutsa mchipsinjo chachikulu, makamaka chifukwa chosalidwa ndi amayi anzake ngakhale abambo apakhomo, moti ena banja mpaka limatha.
Amasalidwa mnjira yanji, kapena matendawa ndi opatsirana? Ayi, matendawa si opatsirana koma amayamba malingana ndi zichitochito zina pamoyo wa munthu, makamaka pazokhudzana ndi uchembere. Mayi amagwidwa ndi matendawa malingana ndi momwe wayendetsera moyo wake wa uchembere, koma palibe mwayi woti wina akagwidwa akhoza kupatsira anzake, ayi.
Ndiye chomusalira nchiyani? Poyamba mukuyenera kumvetsetsa kuti nthendayi ndi nthenda yanji ndipo imachita zotani. Imeneyi ndi nthenda yokhudza njira ya amayi. Pazifukwa zina, njirayi imapezeka kuti yabooka ndiye mkodzo ukamabwera umangodutsa nkumachucha, mwinanso nkusakanikirana ndi chimbudzi. Pachifukwachi, mzimayi amamveka fungo kwambiri moti pagulu la anzake amasowa mtendere komanso anzake amamuthawa. Chomwechomwechonso, abambo a kunyumba amatha kupirira kwa kanthawi koma pena amatopa nkuchoka pakhomopo. Si nkhani yamasewera, ayi, makamaka kwa mayi yemwe wagwidwa ndi matendawo.
Mwangoti pazifukwa zina, kodi simungatambasuleko zina mwa zifukwazo? Ndikufotokozerani zifukwa zitatu zomwe ndi zikuluzikulu muno mMalawi. Pali uchembere olawirira. Munthu akatenga pakati ali wamngono, ziwalo zake zimakhala kuti sizidakhwime ndiye chifukwa chokakamiza pobereka, vuto lotere likhoza kubwera. Njira ina nkubereka pafupipafupi, ziwalo zimatopa mpaka nthawi imadzakwana yoti vuto laonekera komanso njira ina ndi kukonda kuchirira kwa azamba chifukwa pakabwera vuto panthawi yochira, azamba amalephera machitidwe ake.
Ndiye mwati vutoli ndi lalikulu mdziko muno, palibe njira yothandizira amayi oterewa? Njira ilipo yomwe nkuthamangira kuchipatala basi. Mdziko muno muli zipatala zingapo komwe kuli madipatimenti othandiza pavutoli koma anthu ambiri amatsogoza kuti matendawa amabwera kaamba kolodzana moti amataya nthawi nkumayendayenda mwa asinganga mmalo moti athamangire kuchipatala akalandire thandizo zinthu zisadafike poipitsitsa.
Nanga kungoti zipatala, osatiuzako kuti ndi kuti kuli zipatalazo? Zina mwa zipatala zomwe zikupereka nawo thandizo kwa amayi omwe ali ndi nthendayi ndi Queen Elizabeth Central Hospital (Quech) mumzinda wa Blantyre, Zomba Central Hospital ku Zomba, Bwaila ku Lilongwe, Mzuzu Central Hospital ndi Monkey Bay.
| 6 |
Ana ndi Ofunika Pobwezeretsa Chilengedwe-BT Archdiocese Arkdayosizi ya Blantyre yati ana mu mpingowu ndi ofunika kwambiri pa ntchito yobwezeretsa za chilengedwe.
Wachiwiri kwa mlembi wa za utumiki mu arkidayosiziyo, bambo Peter Kamtembe ndi omwe alankhula izi lachisanu ku parish ya Mtenje atatsogolera ana pa ntchito yobzala mitengo yomwe inatsogoleredwa ndi ofesi ya mabungwe a utumiki wa apapa ya Pontifical Mission Societies PMS mu arkdayosiziyi.
Maepiskopi a katolika kuwonetsa kudzipereka kwawo posamalira chilengedwe Bambo Kamtembe ati arkdayosiziyi yazindikira kufunika kogwiritsa ntchito ana achichepere pobwezeretsa za chilengedwe zomwe ati zithandiza anawa kukhala ndi chikhalidwe chobwezeretsa ndi kusamala za chilengedwe ku madera awo chaka ndi chaka.
Mmau ake mmodzi mwa aphunzitsi a utumwi wa ana mparishi ya Mtenje mayi Zita Makunje ati achita chotheka kuonetsetsa kuti anawa akusamalira mitengo yomwe abzala.
| 18 |
Zionetsero zilipo la chiwiri pa 13 January Wamenyetsa nkhwangwa pamwala: Mtambo Zafika pa payerepayere. Mabungwe 20 omwe si aboma amenyetsa nkhwangwa pamwala ponena kuti zivute zitani palibe chomwe chingalepheretse zionetsero za dziko lonse zomwe akonza kudzachita Lachiwiri likebwerali ati pofuna kuonetsa mkwiyo ndi mmene zinthu zikuyendera mdziko muno.
Imodzi mwa nkhani zikuluzikulu zomwe zakwiyitsa mabungwewa ndi ndalama zomwe bungwe loyendetsa ntchito zolimbana ndi matenda a Edzi la National Aids Commission (NAC) lidapereka kumagulu omwe sakhudzidwa pankhondo yolimbana ndi matendawa.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mneneri wa mabungwe omwe akukonza zionetserozi, Timothy Mtambo, yemwe ndi mkulu wa bungwe la Centre for Human Rights and Rehabilitation (CHRR), adati cholinga cha zionetserozi nkudzudzula boma ndi mmene likuyendetsera zinthu zomwe adati zikupweteketsa Amalawi.
Mwa zina, mabungwe omwe si abomawa akuti sakukhutira ndi momwe chuma cha boma chikuyendera, kuchepa kwa chitetezo ndi kusalemekeza ufulu wa Amalawi.
Iwo atinso boma likuwonetsa kuphangira mphamvu posalemekeza nthambi zina za boma monga nthambi ya zamalamulo, zomwe zidayambitsa sitalaka ya nthambiyi ndipo anthu ambiri akuzunzika mndende kudikira milandu yawo.
Mabungwewa akudzudzula nkhani ya ndalama zokwana K5 miliyoni zomwe bungwe la NAC lidapereka kubungwe la mayi wa fuko Gertrude Mutharika la Beautify Malawi (Beam) ndi zomwe lidaperekanso ku gulu la Muhlakho wa Alhomwe.
Koma pomwe mabungwewa akukonza izi, mabungwe ena omwenso si aboma monga bungwe la achinyamata la Youth Empowerment and Civic Education (Yece) ati iwo sadzatenga nawo mbali paziwonetserozi.
Mkulu wa bungweli, Lucky Mbewe, wati omwe akukonza zionetserozi sadatsate njira yoyenera posafunsa maganizo a mabungwe ena.
Zinthu ngati izi zimafunika kukambirana osati kungobwera ndi maganizo omangamanga kuti tichita zakuti ayi. Zimenezi nzomwe zatipangitsa ife kuti tisatenge nawo mbali, adatero Mbewe.
Koma Mtambo akuti mabungwe omwe akupatuka akugwiritsidwa ntchito ndi boma kuti asokoneze zionetserozo.
Mavenda a ku Lilongwe nawo ati sakugwirizana ndi ganizo lodzachita zionetsero polingalira zomwe zidaoneka pazionetsero zamtunduwu zomwe zidachitika pa 20 July 2011.
Zomwe zidachitika pa 20 July 2011 zimatipatsabe mantha moti apa sitikufuna kutenga nawo mbali. Vuto lina ndi lakuti zikakhala chonchi malonda athu amasokonekera ndiye ife ayi, adatero James Yelayela Soko, venda wakalekale, yemwe adatsogolerapo mavenda a mumzinda wa Lilongwe.
Atafunsidwa ngati akudziwapo kanthu pa zionetsero zimene zikukonzedwazi, mneneri wa likulu la polisi Rhoda Manjolo adati apolisi sadalandire pempho lililonse la munthu kapena gulu lofuna kupanga zionetsero.
Mneneri wa Khonsolo ya Lilongwe Tamala Chafunya Lachiwiri lapitali adati ofesiyi sidalandire kalata iliyonse yopempha kuti anthu adzachite zionetsero.
Poikapo maganizo ake, katswiri wa zandale Blessings Chinsinga adati zionetserozo si zolakwika chifukwa ndi njira imodzi yodzudzulira pomwe boma likulephera.
Iye adati mabungwe omwe si aboma ndi ntchito yawo kuonetsetsa kuti boma silikuphotchola pakagwiridwe kake ka ntchito ndiye ngati zinthu zikupotoka iwo akuyenera kupeza njira yowongolera.
Iye adati njira yabwino yowongolera mokhota nkukambirana koma ngati njirayi yakanika mabungwe ayenera kupeza njira zina monga kukonza zionetserozo.
Mkulu wa bungwe loyanganira mabungwe onse omwe si aboma la Congoma, MacBain Mkandawire, adakana kunenapo ngati bungwe la Congoma likugwirizana kapena kutsutsana ndi ziwonetserozi.
Iye adati bungweli lili mkati mwa zokambirana ndi mabungwe omwe akukonza ziwonetserowo kuti aunike ngati nkofunika kutero kapena ayi.
Mafumu nawo aperekapo maganizo osiyanasiyana pankhaniyi.
Mfumu Liwonde ya ku Machinga idati kuchita zionetsero nkutaya nthawi chabe chifukwa palibe phindu lomwe limaoneka.
Koma Inkosi Chindi ya ku Mzimba idati ngati anthu akuona kuti penapake sipadayende bwino ali ndi ufulu kuchita zionetserozo kuti aonetse kusakondwa kwawoko ndipo polakwikwapo pakonzedwe.
Nayo T/A Nkukula ya ku Lilongwe idati ngati magulu okhudzidwawa adakambirana pazolakwikazo nkulepherana, zionetsero nzosalakwika.
| 11 |
Aziputa dala Amuna ambiri amakonda zongotenga asungwana osawadziwa nkukagona nawo ku maresitihausi.
Zikatha bwino, amaoneka wochenjera. Komatu amaiwala kuti nthawi zina akhoza kugwa nazo mmavuto oopsa.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Tsikulo, Katakwe adali paulendo wobwerera ku Lilongwe kuchokera ku Blantyre pomwe adamuona msungwanayo. Pagulu la anthu omwe adali pasiteji ya basiyo, mwana wamkazi adawala ngati duwa pakati pa zinyatsi.
Phazi la Katakwe lidagwa pa buleki mosaliuza. Adaima chapatsogolo nakodola msungwanayo. Msungwanayo sadanyamuke nthawi yomweyo.
Adatulutsa kagalasi mchikwama chake cha mmanja ndikupaka kaye lipisitiki milomo yake. Kenaka adaponya magalasi akuda mmaso mwake.
Adayenda modzithyola ngati ali pa catwalk. Wamtalipo, msungwanayo adali mdiresi lothina, lalitali lomwe lidaumba bwino thupi lake.
Atalowa mgalimoto mpomwe Katakwe adaona kuti diresi la namwaliyo lidali ndi siliti yofika mpaka muntchafu.
Katakwe adazunguzika mutu. Mmoyo mwake adali asadaonepo msungwana wokongola ngati namwaliyo.
Mumtima adadzitsimikizira kuti ayenera kutulutsa mawu a kukhosi asadafike ku Lilongwe.
Galimoto lidadya mtunda, uku awiriwo akucheza. Msungwanayo adati dzina lake lidali Jo.
Katakwe adapeza kuti msungwanayo amachitako kachakumwa koledzeretsa ndipo iwo ankaima mmalo osiyanasiyana nkumakonkhako ka mowa. Mmene ankayandikira ku Lilongwe nkuti atathodwa ndithu.
Katakwe sadatulutse mawu a kukhosi komabe nkucheza kwawo kudapezeka kuti awiriwo adagwirizana zokagonera limodzi ku resitihausi.
Atafika mu Lilongwe adapita kumalo angapo achisangalalo ndipo mmene nthawi imafika pakati pa usiku adapita kukagonera limodzi ku resitihausi.
Adayamba kudzuka adali Katakwe. Adakasamba kubafa. Pobwera anadabwa kuona msungwana uja asadadzukebe. Adamugwedeza. Mwana wamkazi adangoti thapsa.
Adamugwedezanso msungwanayo. Ulendo uno mwa mphamvu. Msungwana adangoti lobodo! Apa mpomwe Katakwe adazindikira kuti kena kake kavuta. Ndi mtima wozama adaona kuti msungwana adali atamwalira.
| 15 |
Kusamala nazale ya fodya Pamene alimi ali pakalikiliki kusosa, alimi, makamaka a fodya ali mmalingaliro okonza nazale.
STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi mtsogoleri wa alimi a fodya omwe ndi mamembala a bungwe la Tobacco Association of Malawi (Tama) ku Bolero mboma la Rumphi Isaac Msiska za kusamalira nazale. Adacheza motere: Escom in free-for-all fuel scam Wait gets longer Secrecy over party funders Tandifotokozerani kuti pokonza nazale ya fodya mlimi amayenera kuyangana zinthu ziti? Choyamba, popanga nazale ya fodya nkupeza malo omwe ali pafupi ndi madzi chifukwa nazale ya fodya imafuna kuthirira kawiri tsiku lililonse osaphonyetsa. Pamafunika kuthirira mmawa kenako madzulo ndiye ngati yatalikirana ndi madzi, pali vuto lalikulu zedi pamenepo.
Alimi amayenera kuyanganira bwino fodya pa nazale Malo apezeka, chotsatira nchiyani? Malo akapezeka pamafunika kuonetsetsa kuti mpofewa. Ngati pali polimba, ntchito ya madzi ija imayambira pamenepo kuwazapo kuti pafewe kenako nkugaulapo bwinobwino. Tikatha kugaula, timayikapo zinyalala nkutentha kaamba kuti ngati mnthaka mumakhala njere za mbewu zina zomwe sizifunika kumerera limodzi ndi fodya zife.
Zonsezi zatheka chimatsatira nchiyani? Iyi ndinthawi yoyamba kupanga mabedi ndipo popanga mabediwo palinso zina zomwe timayenera kutsatira. Timatenga madzi nkuthiramo mankhwala omwe amathandiza kupha kapena kuthamangitsa Nyerere zomwe tikazilekerera zimakoka njere tikabzala. Tikawazapo, timapanga mabedi a nazale ya fodya kuyembekezera kuti nthawi ina iliyonse tifesa fodya panazale.
Tsiku lofesa kumakhala zotani? Tsiku lofesa pamafunika kuti zinthu zonse zofunikira ngati zija ndalongosolazi zikhale pafupi koma china chomwe sindidanenepo ndi udzu waa kansichi otchingira pamwamba pa mbewu zathu. Udzuwu ndi wachilengedwe koma umayenera kukhala pafupi oduladula kale kuti tikangofesa, nthawi yomweyo titchinge pamwamba.
Mumafesa bwanji? Choyamba kansichi wathu ali apo, timatenga kheni yothiririra nkuyikamo madzi ndi mbewu ya fodya nkumachita ngati tikuthirira ndiye mbewu zimatulukira limodzi ndi madzi aja. Tikatha timatchingira bwinobwino ndi kansichi uja. Tikatero, ntchito yothirira yayambika ndipo timati uku tikuthirira nazale, kwinaku tikukonza kumunda kupangiratu mizere kuti tizichepetsako ntchito ina pangonopangono.
Nazale yabwino imafunika kukhala ndi mabedi angati? Nazale ikhoza kukhala ndi mabedi angapo koma pamakhala bedi limodzi lomwe limakhala kholo. Zonse timafesa pabedi la kholo lija pofuna kuchepetsa ntchito malinga ndi zomwe ndanena kuti pamakhala kuthirira mwakathithi. Mbande zikakula pangono, timazisamutsira pa mabedi ena aja kuti zizipuma bwino koma kuthirira mwakathithi kumapitirirabe.
Nzololedwa kubwereza malo a nazale potengera kuti malo opezeka madzi ndi wovuta? Nzosaloledwa kubwereza malo a nazale. Mbewu zina zimakhala ndi matenda akeake ndiye mukachotsapo, matenda kapena tizilombo timatsalira pamalopo choncho podzabzala mbewu Inayo imakumana ndi vutoli ikadali yaingono kwambiri nkuvutika kakulidwe.
| 4 |
Mphwiyo, Kasambara akadali mchitokosi Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Pamene bwalo la milandu ku Lilongwe likupitiriza kumva nkhani za amene akuwaganizira kuti adatengapo gawo posolola ndalama za boma, yemwe adali woyendetsa chuma cha boma Paul Mphwiyo komanso nduna yakale ya zachilungamo Ralph Kasambara akadali mchitokosi.
Akadali mkati: Mphwiyo Kasambara akuyankha mlandu womuganizira kuti adakonza chiwembu chofuna kupha Mphwiyo pamene Mphwiyo akuyankha mlandu womuganizira kuti adatengapo gawo poba K2.4 biliyoni ya boma. Iye adamangidwa Loweruka lapitalo pomwe oganiziridwa ena pamlanduwo Auzius Kazombo Mwale, Clemence Mmadzi ndi Roosevelt Ndovi adatulutsidwa pabelo Lachitatu.
Lachinayi, wachiwiri kwa mkulu wa bungwe lothana ndi ziphuphu la Anti-corruption Bureau (ACB) Reyneck Matemba yemwe amaimira boma pamlanduwo mmalo mwa mkulu wa oimira boma pamilandu Mary Kachale adapempha wogamula Esmie Chombo kuti Mphwiyo asungidwebe mchitokosi kwa sabata ziwiri.
Apolisi ofufuza za ndalama apeza maumboni ena okhudzana ndi Mphwiyo ndipo potha sabata ziwiri akhala atamaliza zofufuza zawo. Ngati adzakhale asanamalize, tidzalola kuti atuluke. Sikuti tikungofuna kumuzunza, adatero Matemba.
Mphwiyo ali ndi milandu 17 yokhudza zosololazo.
Ndipo woweluza kubwalo lalikulu la Lilongwe Rezine Mzikamanda dzana adati pofika Lachisanu sabata ya mawa, Kasambara adzakhala atadziwa ngati angatuluke kapena ayi. Izi adanena woimira Kasambara Modecai Msiska adapempha bwalolo kuti litulutse Kasambara chifukwa woweluza Michael Mtambo adabweretsa nkhani yoti Kasambara asakhalenso pabelo kukhoti yekha nkulamula kuti Kasambarayo alowenso mchitokosi.
| 7 |
Anatchezera Ndimamukonda Agogo, Ndinali pachibwenzi ndi mkazi wina ndipo zaka ziwiri zatha pomwe tinasiyana. Pano ali ndi mwana yemwe wabereka mwezi watha ndiye akumabwera kwa ine nkumati tibwererane. Kodi pamenepa ndithani, agogo? Mkaziyo kunena zoona ndimamukonda, koma pano ndinalimba mtima. Nditani? Ine Amfumu, Zingwangwa Amfumu, Nkhani yanu ndi yovuta kuitsata bwinobwino chifukwa simukumasula kuti vuto lanu ndi chiyani jwenikweni. Poyamba mwanena kuti mkaziyo munasiyana naye zaka ziwiri zapitazo, munasiyana chifukwa chiyani? Mwati pano mkaziyo akuti mubwererane ndipo inu nomwe mukuti kunena zoona ndimamukonda. Komanso inu nomwenso mukuti pano munalimba mtima, mukutanthauzanji? Mwatinso mkaziyo ali ndi mwana wa mwezi umodzi, nchachidziwikire kuti mwanayo si wanu-poti mwanena nokha kuti chibwenzi chanu chidatha zaka ziwiri zapitazo. Apatu, kunena zoona Amfumu, mayankho muli nawo ndinu. Ngati mkaziyo mukuti mumamukonda, chovuta nchiyani kuti mubwererane? Koma mukuti mwalimba mtima, kulimba mtima kotani? Nchifukwa chake ndikuti zonse zili ndi inu kuti mubwererane kapena ayi poti zifukwa zake zomwe mudalekanirana mukuzidziwa ndinu. Mwakula mwatha, Amfumu.
Chisale watuluka nkumangidwanso Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Akufunabe wakale? Agogo, Ndili ndi mkazi yemwe ndabereka naye ana atatu koma nthawi zambiri wakhala akumafunabe chibwenzi chake chakale chomwe chidamusiya. Ndakhala ndikupeza ma SMS olemba I LOVE U MPAKA KALE pafoni. Ndikamufunsa amathamangira kupepesa. Kodi andithandiza ameneyu? Ndinganene kuti ndidapezadi mkazi kapena ndiyangane wina? Chonde ndithandizeni.
Ine Che Mwenye Che Mwenye, Pa Chichewa pali mawu oti madzi saiwala khwawa. Mawuwa akutikumbutsa kuti pali anthu ena amene akakhala pachibwenzi, ngakhale chibwenzicho chitatha akakumana amakumbutsa chikale; amathanso kumachitirana nsanje, chonsecho chibwenzi adathetsa pakati pawo. Mchitidwe kapena khalidwe lotere silofunika anthu mukakhala mbanja chifukwa tanthauzo lake nloti wina akuzembera mnzake wabanja pokhala ndi chibwenzi kapena zibwenzi zamseri. Wina akangozindikira kuti mnzangayu akundiyenda njomba, ukwati nthawi zambiri sulimba.
Tsono apa kunena mwachindunji, mkazi wanuyo alibe chilungamo chifukwa sangamalembe kapena kulandira ma SMS achikondi kwa wina inu mulipo. Malamulo a mbanja amakana zimenezi, chifukwatu munthu wotere sunga mukhulupirire. Banja lagona pachikondi ndi chikhulupiriro kwa wina ndi mnzake.
Komanso inu, abambo, muli ndi vuto. Akazi anu akachokapo basi muli pafoni gwi! kuyangana kuti waimba ndani kapena kumayangana ma SMS. Si bwino kumatero chifukwa zimaonetseratu kuti mbanja mwanu simukhulupirirana.Chomwe mungachite apa ndi kukhala pansi ndi akazi anu kuwafotokozera bwino lomwe za kuipa komagonekerana khosi ndi bwenzi lawo lakale pomwe tsopano ali ndi inu. Ngati akupiririzabe mchitidwe wotere, muli ndi zifukwa zokwanira zothetsera banja chifukwa mkazi sakhala ndi mitala. Pajatu amati mapanga awiri avumbwitsa.
| 15 |
Akufuna mwana Akufuna mwana Zikomo Gogo Banja ndi mwamuna wanga lidatha mu 2011. Ndidapeza mwamuna wina yemwe timamvana ndipo tidakayezetsa komwe adatipeza kuti tilibe kachilombo koyambitsa Edzi. Vuto ndi lakuti bwenzi langalo limakonda zogonana komanso limandiletsa kuchita za kulera. Wina adandiuza kuti bwenzi langalo lili ndi mkazi koma nditamufunsa adakana. Tsiku lina ndidaimba foni 5 koloko mbandakucha ndipo ndidamva kulira kwa mwana wakhanda. Nditamufunsa adakana ndipo adati ndi wa khomo loyandikana nalo, nadula foni nthawi yomweyo. Ndizimukondabe? R, Chiradzulu R, Mwakumana ndi chilombo cha bodza. Wakunamizani kuti akufuna mwana chonsecho pansi pa mtima akudziwa kuti akakupatsani mwana adzakuthawani nkupitiriza kukhala ndi mkazi wake. Wakunamizaninso kuti mwana amalira ndi woyandikana nawo nyumba. Ngati zili zoona, bwanji adadula foni? Asakutayitseni nthawi ameneyo.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Ndimamupitirira Wawagogo, Ndili ndi zaka 17 ndipo pali mnyamata wina wa zaka 20 yemwe akundifuna. Ndimamukonda koma vuto ndi lakuti iyeyo ndi wamfupi kuposa ine. Ndimachita manyazi ndikamayenda naye. Ndimulole? C C, Sindikuonapo vuto loti musamulolere! Kutalika kukhale nkhani? Chikondi chimachoka mumtima ndipo sichiyenera kuona ngati wina ndi wamtali kapena wamfupi, woonda kapena wonenepa, woona kapena wosaona ndi zina zotero. Chabwino nchiyani kuti mudzapeze mnyamata wamtali ngati inu kapena kukuposani koma alibe chikondi kapena kukhala ndi mwamuna ameneyu yemwe amakukondani nanunso mukumukonda? Muloleni ameneyo basi.
Amakonda ndalama Anatchereza, Ndakhala paubwenzi ndi msungwana wina koma vuto lake akuoneka wokonda ndalama. Tikangokumana, amandipempha ndalama. Timalankhulana nthawi zambiri pafoni koma mwezi ukangotha amati tikumane. Kodi ichi ndi chikondi? M, Lilongwe.
M, Ameneyo sakuthandizani. Mkazi woika ndalama patsogolo si wabwino. Taonani akuonetsa mawanga ake muli pachibwenzi nanga mukadzakwatirana zidzatha bwanji? Mudzaona kuti pakati pa mwezi mavuto okhaokha mbanja. Koma ukangotha mwezi sikusekerera kuchitsakano kwake. Mpeweni.
Mtendere palibe Kuyambira pomwe tidalowa mbanja, sitinathe mwezi tili pamtendere. Iye amati ine si mwamuna amene iye ankakhumba. Iyetu ndi wobadwanso mwatsopano ndipo akati agwe ndi pemphero, mukhoza kuona kuti ayi, mayi amapemphera uyu. Iye amati zivute zitani tidzasiyana basi. Kodi ndidikire adzandisiye, kapena ndilowere kwanga? Inetu ndimamukonda! M, Blantyre.
| 15 |
Nkhoma yakhumudwitsa DPP, UTM Zipani za Democratic Progressive Party (DPP) ndi UTM zati zakhumudwa ndi kalata yomwe Sinodi ya Nkhoma ya mpingo wa CCAP yatulutsa sabata yatha.
Kalatayo, yomwe siidatchule dzina la mtsogoleri aliyense, ikufotokozera Akhristu ampingowo munthu woyenera kudzamuvotera.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kaliati: Nkhoma yalakwa Kalatayo ikuti mtsogoleri woyenera kumuvotera ndi yemwe ali wodzadzidwa ndi Mzimu Woyera, wangwiro, wokonda chitukuko, wosasankha anthu potengera mitundu yawo, komanso yemwe ali ndi chidwi chothana ndi katangale.
Nduna yofalitsa nkhani, Henry Mussa, adati mpingowo usaiwale kuti mmbuyomu nawonso udakhudzidwa ndi nkhani za ziphuphu ndi katangale.
Mchaka cha 2014 ena mwa ogwira ntchito ku Sinodi ya Nkhoma adanyambita K61 886 389.11 ya ntchito zachitukuko. Boma la America ndilo lidapereka ndalamazo kudzera bungwe lake la chitukuko la United States Agency for International Development (USAaid).
Mlembi wa Nkhoma pa nthawiyo, mbusa Vasco Kachipapa, adavomera kuti zinthu zidalakwika ndipo Sinodiyo idabweza ndalamazo.
Membala wa mpingo kapena chipembedzo chilichonse chili ndi ufulu wopikitsana nawo pa mpando uliwonse wa ndale. Choncho nkulakwa kuti mpingo uzisiyanitsa anthu kuti ena ndiwoyera kuposa anzawo, kalata yomwe boma latulutsa ndipo yasayinidwa ndi Mussa yatero.
Ndunayi idati mfundo za Sinodiyo zangokolanakolana mkalatayo.
Naye mlembi wa UTM, Patricia Kaliati, adati zomwe yachita Sinodiyo pouza mamembala ake kuti atsogoleri ena ndi woyera poyerekeza ndi anzawo nkulakwa, komanso nzogawanitsa anthu.
Tikayamba kufukulana, kodi pakhala zabwino? Mtsogoleri aliyense kuti tiyambe kumuunika mbiri yake, kodi woyera mtima apezekapo ngati momwe ikulankhulira Sinodiyo? Zinazi tiyeni tiziweruza ndi mtima wangwiro, adatero Kaliati.
Iye adati Sinodi ngati mpingo idayenera kuuza nkhosa zake kuti zisafooke mmapemphero, kupembedzera dziko lino kuti zisankho zidzayende bwino osati kubzala mbewu zamipatuko mitima mwawo.
Mkalata yake Sinodi ikuti boma silikuonetsa chidwi pofufuza kuphedwa kwa mnyamata wa ku Polytechnic Robert Chasowa, mmodzi mwa akuluakulu a Anti-Corruption Bureau (ACB) Issa Njauju ndi Buleya Lule yemwe amakhudzidwa ndi nkhani yodzembetsa mwana wachialubino.
Mbusa wamkulu mu Sinodiyo, mbusa Bizwick Nkhoma, adati mpingo wake umalembera Akhristu ake kalatayo osati chipani chilichonse. Choncho sangayankhe pa zomwe anthu kapena chipani chilichonse chikulankhula.
| 11 |
Mkulu wa zaka 22 akaseweza zaka 23 Wakhala akuthyola nyumba masana kasanu konse ndi kubamo katundu. Anthu ku Balaka akhala akumusaka koma adali woterera ngati mlamba. Koma la 40 lamukwanira John Bunaya, wa zaka 22, amene bwalo la milandu lamuthowa ndi zaka 23 kuti akaseweze kundende chifukwa cha kutolatola.
Wapolisi woimira boma pamilandu, Inspector Isaac Mponela, wati bwalo la Balaka lidapeza mkuluyu wolakwa pamilandu yonse isanu yomwe adapalamula.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mponela adauza bwalolo kuti pa 3 March, chaka chino, masanasana dzuwa likuswa mtengo, Bunaya adaswa nyumba ya Gloria Mphwiyo ndi kubamo njinga ya komanso matumba awiri a chimanga. Zonse zidali za mtengo wa K43 000.
Pa 28 March, chaka chonchino, Bunaya akutinso masanasana adaswa nyumba ya Ruth Marley ku Majiga mbomalo ndi kubamo wailesi komaso zovala ndi katundu wina.
Bunaya pa 13 April, akuti adaphwanyanso nyumba ya Rachel Jika ndi kubamo laputopu, matilesi, mafuta ophikira ndi shuga za K320 000.
Pa 10 May, Bunaya akuti adaswa nyumba ya William Munthali ndi kubamo kamera, foni ndi zakugolosale za K72 000.
Iye sadalekere pomwepo. Pa 13 May akuti njondayi idakaswanso nyumba ya Daniel Pondani komwe adakasokolotsa DVD, masipika awiri a LG, mafuta ophikira ndi mafoni za K100 000.
Mponela atamaliza kumunenera Bunaya kubwaloko, anthu adadzidzimuka. Izi zidadabwitsanso woweruza milandu, Victor Sibu, yemwe sadachedwe koma kusatakula chilango chokhwima.
Iye adalamula Bunaya, yemwe adavomera kulakwa pamilandu yonseyi, kuti akaseweze zaka 23 ngakhale iye adaliralira kuti ndi wachichepere komanso ndiye amasamala banja lake ndi makolo omwe adati ndi okalamba.
Bunaya amachokera mmudzi mwa Kandengwe kwa T/A Nsamala mbomalo.
| 7 |
Chitamponi kanthu pa za fisp Wapampando wa komiti ya zaulimi mNyumba ya Malamulo, Felix Jumbe, wati boma lichitepo kanthu pa za mmene ndondomeko ya Farm Input Subsidy Programme (Fisp) ya zipangizo zaulimi zotsika mtengo ikuyendera polingalira kuti nthawi ikutha.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Jumbe adalankhula izi pocheza ndi Uchikumbe potsatira lipoti la pa 5 January la mmene ntchitoyi ikuyendera lomwe likusonyeza kuti kufika pano, pamatumba 100 alionse a feteleza, 76 okha ndiwo adafika kumalo ogulitsirako zipangizozi.
Ngakhale ena agula kale zipangizo, madera ena sizidafike Malingana ndi Jumbe, iyi ndi nkhani yoopsa chifukwa mbewu zimakhala ndi nyengo yake yomwe zimachita bwino zikalandira feteleza ndipo kuti kuthira feteleza nyengoyi itadutsa kale sikungapindule kanthu kwa mlimi.
Fetelezatu sangothirapo poti wapezeka ayi. Pali nyengo yake malingana ndi mmene mbewu zikukulira chifukwa zikadutsa pena pake, kuthira feteleza kumangokhala kuononga chabe.
Mwachitsanzo, munthu ungamathire feteleza wokulitsa chimanga chitayamba kale ngaiyaye nkumati ukuchitapo kanthu? Mwezi wa January alimi amayenera zipangizo ali nazo pafupi, adatero Jumbe.
Nyuzipepala ya The Nation ya pa 8 January idasindikiza kuti zotsatira za mkhumano wa pakati pa nduna ya zamalimidwe, ulimi wamthirira ndi chitukuko cha madzi, Allan Chiyembekeza, ndi eni makampani omwe zikunyamula zipangizozi, adagwirizana kuti ntchitoyi ikuyenera kutha pofika pa 31 December, 2015.
Malingana ndi Jumbe, pomafika pa 5 January ntchitoyi inali ikadali mkati zikusonyeza kuti pena pake pali vuto mndondomekoyi ndipo mpofunika kuti akuluakulu omwe akuyendetsa ntchitoyi achitepo kanthu msanga.
Nduna ya zachuma ndi chitukuko, Goodall Gondwe, adauza nyuzipepala yomweyi kuti anthu akupupuluma kufalitsa zolakwika za pulogalamuyi zomwe zikusemphana ndi momwe ikuyendetsedwera chaka chino.
Iye adati nzomvetsa chisoni kuti zaka zingapo chiyambireni pulogalamuyi, anthu ena amaganizabe kuti idayambitsidwa ndi cholinga chothetsa umphawi pomwe cholinga chake nchakuti anthu azikhala ndi chakudya chokwanira.
Cholinga cha pulogalamuyi nchakuti anthu azikolola chakudya chokwanira koma anthu ena amaganiza kuti idabwera kudzathetsa umphawi. Maganizo otere ndiwo amachititsa kuti anthu aziyembekeza kuthandizidwa chaka ndi chaka, adatero Gongwe.
| 11 |
Anatchezera Akumandiipitsa Zikomo agogo, Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndili ndi chibwenzi ndipo makolo akudziwa ngakhale kuti ndi mwamphekesera chabe. Nthawi ina bambo ake (osati omubereka) amafuna kumugwiririra ndiye akumandiipitsa dzina kwa mayi ake, koma iwo sakutekeseka ndi izi. Ndili ndi mantha, nditani pamenepa agogo? FK, Mchinji FK, Wati uli ndi mantha, mantha ake otani? Sindikuonapo chifukwa choti uzikhala ndi mantha pamene sudalakwire munthu aliyense. Ndiye iwe ukuchita mantha ndi ndani? Ngatidi ukunena zoona kuti bambo omupeza a mtsikanayo adafunadi kumugwiririra, bwenzi lakolo adachitapo chiyani zitachitika zimenezo? Kodi mayi a mtsikanayo nkhaniyi akuidziwa? Ngati akuidziwa adachitapo chiyani? Ndikufunsa mafunso onsewa chifukwa ndi mlandu waukulu kugwiririra kapena kufuna kugwiririra ndipo munthu wopalamula mlandu wotere amayenera kulangidwa kundende malinga ndi malamulo a dziko lino. Munthu wotere ngosafuna kumusekerera. Ndibwerere kunkhani yako yoti uli ndi mantha. Ngati umamukonda zoona mtsikanayo pitiriza kutero chifukwa tsiku lina udzakhala mpulumutsi wake kwa bambo womupezayo mukadzakhala thupi limodzi. Mwina mayi ake sakutekeseka ndi zokuipitsira dzina lako chifukwa akudziwa choona chenicheni, maka pankhani yoti amuna awo amafuna kugwiririra mwana wawo, koma akukhala chete chifukwa akuopa kuti angawasiye banja. Tazionapo izi zikuchitika.
Akuti tibwererane Zikomo gogo, Ndinali pachibwenzi ndi mtsikana wina kwa miyezi isanu ndi umodzi. Pamene timati tipange ukwati mwezi wotsatira iyeyo adathetsa chibwenzi ndi kutengana ndi wina. Patatha miyezi iwiri adabwera ndi kudzandipepesa ati tibwererane koma akwathu akukana. Kodi nditani pamenepa? NG, Mzuzu NG, Utani pamenepa? Mvera malangizo a makolo ako kapena akwanu amene akuti usayerekeze kubwererana naye chifukwa zimene akukulangizazo ndi zoona. Mawu a akulu amakoma akagonera, ukanyalanyaza udzalirira kuutsi tsiku lina. Iye adathetsa chibwenzi pakati pa iwe ndi iye ndipo adakwatiwa ndi wina kenaka patha miyezi iwiri uyo akubwera poyera ali undikhululukire, tibwererane. Alibe manyazi! Chavuta komwe adakakwatiwako ndi chiyani? Chilipochilipo. Ndiye iwe ukavomereza zoti mubwererane udzaoneka wombwambwana; wodya masanzi.
Ndimukhulupirire? Agogo, Ndili pachibwenzi ndi mnyamata wina wake. Ndakhala naye zaka zinayi. Chaka chino adakaonekera kwathu koma ineyo akundikaniza kuti ndikaonekere kwawo. Ndikamufunsa kuti akundikaniza chifukwa chiyani sayankha zogwira mtima koma ndikamufunsa za ukwati amavomera ndi mtima wake wonse. Ndimukhulupirire? Ine Fannie, Blantyre.
| 12 |
Zulani mitengo ya fodya poopetsa matenda Nthawi ino alimi ambiri a fodya ali kalikiriki kufunafuna mbewu, kukonza malo omwe adzalimepo komanso kukonza ndi kufesa nazale.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Ngakhale izi zili choncho alimi ena mmaboma a Mzimba ndi Rumphi akutsalira pantchitoyi kaamba koti iwo sadazulebe mitengo ya fodya mminda mwawo.
Mlangizi wa za ulimi Lewick Zimba wauza Uchikumbe kuti izi zikhoza kudzaononga fodya munyengo ikubwerayi.
Alimi amayenera kuzula ndi kuotcha mitengo imeneyi akangomaliza kuthyola fodya wawo kuti aphe tizilombo tonse tomwe tingakhale mumitengoyo.
Fodya ali gulu limodzi ndi tomato ndi mbewu zina zomwe sizichedwa kugwidwa ndi matenda ndipo mitengo ija ikasiyidwa kwa nthawi yaitali mmunda umasanduka malo omwe tizilombo timasweranamo,adatero Zimba.
Zimba adati madera amasiyana nyengo yokolola fodya. Madera a kummwera ndi pakati amayenera kuyambirira kuzula pomwe madera a kumpoto amamalizira ngakhale nthawi yake madera onsewa ndi miyezi ya March mpaka April, adatero Zimba.
Iye adati alimi omwe sadazule ndi kuotcha mitengo ya fodya mminda mwawo akuyenra kutero nthawi ino ngati akufuna kudzapindula ndi fodya wawo nyengo ikudzayi.
Fodya amafunika chisamaliro chokwanira ndipo chisamaliro chimenechi chimayamba mlimi akangokolola fodya wake mmunda, adatero Zimba.
Iye adati alimi akuyenera kuzindikira zomwe akuyenera kuchita ndi nthawi yomwe akuyenera kutero kupewa kulakwitsa kapena kusokoneza zomwe zikadatha kupeweka.
Alimi akuyenera kumvera alangizi komanso ngati apali zinthu zomwe sakumvetsetsa akuyenera kufunsa kwa alingizi a kudera lawo, iye adatero.
Mlangiziyu adati Malawi ndi dziko lomwe limadalira ulimi wa fodya pobweretsa ndalama za kumaiko akunja kotero nkofunika kuti fodya azisamalidwa bwino kuti phindu lake lizioneka pokhala kuti mbewuyi imafuna ntchito yambiri.
Amon Gondwe, mmodzi mwa alimi amene mpaka pano sanazulebe mitengo ya fodya mboma la Rumphi, wati ntchito imawakulira kuti ayambe kuzula nthawi yomwe amaliza kuthyola fodya.
Timati tidzazulabe kenaka mpaka kumapezeka kuti nthaka yauma ndipo mitengoyi imalimba ndiye timangozisiya, adatero Gondwe.
Iye adati akudziwa za ubwino wozula mitego ya fodyayo akangomaliza kukolola, makamaka potengera kuti ntchito imachepa, koma kwina kumakhala kutayirira kumbali ya alimi, amene ambiri mwa iwo amafuna adzipepese kaye akangogulitsa fodya wawo.
| 4 |
Nyumba ya Delamere Yapsa Munthu mmodzi wavulala pa ngozi ya moto umene unabuka pa chinyumba chosanjikizana cha Delamere mu mdzinda wa Blantyre.
Nyumba ya Delamere ikuyaka moto Wofalitsa nkhani za apolisi mu mzinda-wu Augustus Nkhwazi watsimikiza za nkhaniyi ndipo wati ngozi-yi yachitika lero mmawa. Iye wati pa ngozi-yi katundu wambiri wasakazika koma kuti ntchito yofufuza gwero la ngozi-yi ili mkati.
Motowu unayamba cha mma 7 mamawa ndipo unakhudza gawo lomwe kukukhala a Kachere Institute of Health and Development, anatero a Nkhwazi.
Iwo ati mkulu amene wavulalayu Micheal Wataya yemwe ndi wowerengetsera ndalama wa Delemere Properties wagonekedwa pa chipatala cha Blantyre Adventist mu mzinda omwewo wa Blantyre.
Pamenepa Nkhwazi walimbikitsa anthu a mu mzindawo kuti azikhala tcheru komanso osamala pofuna kupewa ngozi za moto ngati izi zomwe wati zikuchulukira kwambiri mu mzindawo pa zifukwa zosiyanasiyana.
| 14 |
Alimi samalani pososa Mlimi weniweni ndiye amasamalitsa kalendala yake ya ulimi. Kuyambira mwezi watha mpaka uno, alimi amalangizidwa kuti akuyenera kuyamba kusosa.
Mlangizi wamkulu mboma la Chiradzulu, Sheila Kangombe wati alimiwa ayenera asamalitse pamene akusosa chifukwa chiyambi chosakolola zochuluka ndi nthawi yososa.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kangombe adati alimi akuyenera kudziwa kuti mitengo ya thonje ndi fodya siyiyenera kukwiriridwa chifukwa nthawi zambiri imakhala ndi matenda.
Pofotokozapo njira zabwino za kasosedwe, Kangombe adati kukwirira mapesi ndi ndondomeko yabwino ya kasosedwe chifukwa kumasunga manyowa.
Alimi angathe kukwirira mapesi ngati awa Mapesi a chimanga mtedza ndi mbewu zina ayenera akwiriridwe, iyi ndi njira yabwino ya kasosedwe chifukwa zikaolerana zimapanga manyowa.
Ena amakonda kuotcha mapesi, izi siziloledwa koma mitengo ya fodya ndi thonje ndi zomwe ziyenera kuotchedwa. Mapesi achimanga komanso mbewu zina amabweretsa manyowa ngati akwiriridwa, adatero iye.
Madera ambiri alimi ayamba kale kukwirira koma ena sadayambe monga zilili ku Dedza komwe alimi ali otangwanika ndi kukumba kachewere ndi mbatata ya kholowa.
Sylvester Chitini wa mmudzi mwa Salile kwa T/A Kasumbu mboma la Dedza akuti kumeneko alimi sadayambe kusosa komabe mwezi ukudzawu ayambapo.
Pano ndife otangwanika ndi kukumba mbatata ya kholowa komanso kachewere. Nthawi zonse timayamba mochedwa kusosa kuno. Kumapeto kwa September aliyense akhala wayambapo kusosa, adatero iye.
Mboma la Blantyre ndi maboma ena alimi ena akumaliza kusosa pamene ena akuyamba kumene. Tomasi Kandodo wa ku Chilomoni akuti sabata ikubwerayi akhala atamaliza kusosa munda wake.
| 4 |
Chingota, Mulomole Sayimanso pa Chisankho sizes="(max-width: 827px) 100vw, 827px" />Chingota(kumanzere) Mulomole (pakati) atsiriza materemu awo Wapampando wa bungwe la mgwirizano wa mipingo ndi zipembedzo la Public Affairs Committee (PAC) mbusa Dr. Felix Chingota, komanso Mneneri wa bungweli Fr. Peter Mulomole, ati sapikisana nawonso pa chisankho cha bungweli chomwe chichitike mwezi wa mawa.
Polankhula ndi Radio Maria Malawi, bambo Mlomole ati awiriwa sapikisana nawonso mmaudindowa kaamba koti atsiriza materemu awo okhalira pa mipandoyi.
Bungweli likuyembekezeka kuchita chisankho pa 18 komanso 19 December chaka chino.
Bambo Mlomole ati pa zaka 6 zomwe akhala ali pa udindowu, iwo ndi okhutira ndi momwe agwilira ntchito ngati mneneri wa bungweli.
Ndine okondwa kwambiri. Ndagwira ntchito yanga bwino momwe ndikudziwira kuti ndimayenera kugwilira, anatero bambo Mlomole.
Mwazina bambo Mlomole adzudzula anthu omwe amanena kuti bungwe la PAC limakonda kudzudzula kwambiri.
Ife ndi atumiki koma kupemphera aliyense amatero ku tchalitchi kapena ku mzikiti kwake. Tikakumana timakhala tikuona mavuto omwe tikukumana nawo ngati dziko ndi kumadzudzula pomwe sipanayende bwinopo kuti pakonzedwe. Timachita ndipo tizachitabe zimenezi mpaka kalekale sitidzasiya, anatero bambo Mlomole.
Iwo ati amachita izi chifukwa bungweli linakonzedwa mchaka cha 1992 patapezeka mavuto pomwe ma episkopi a mpingo wa katolika anayankhulapo mu ulamuliro wa chipani chimodzi.
| 11 |
Papa Apemhelera Mliri wa COVID-19 Loweruka Mtsogoleri wa Mpingo wa Katolika pa dziko lonse Papa Francisco akuyembekezeka kuchita mapemphero pofuna kuti mliri wa Coronavirus uthe.
Papa anapempheleraponso anthu okhudzidwa ndi Coronavirus mmbuyomu Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican, Papa achita mapemphero a kolona loweruka likudzali mogwirizana ndi malo oyera onse pa dziko lonse la pansi. Ndipo mutu wa mapemphero a Kolonawa ndi Kukhala okhulupirika mmapemphero limodzi ndi Amayi Mari Papa Francisco adzachita mapemphero a Kolonawa pa Grotto la ku Lourdes lopezeka kulikulu la Mpingo ku Vatican.
Mapempherowa omwe adzayambe nthawi ya 5:30 PM nthawi ya ku Rome yomwe ndi nthawinso ya ku Malawi adzauluka pompopompo (LIVE) pa wayilesi ya kanema ku dziko lonse la pansi.
Pa nthawi ya mapempherowa ma grotto akuluakulu pa dziko la pansi adzalumikizananso ndi Papa Francisco kudzera pa makina a intaneti. Ma grottowa ndi Lourdes, Fatima, Lujan, Milagro, Guadalupe, San Giovanni Rotondo komanso Pompeii.
| 13 |
anatchezera Akunyengana ndi mnzanga Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Zikomo Anatchereza, Ndakhala pabanja zaka 7 ndipo tilinso ndi mwana wa zaka 7. Tsiku lina mwanayo adathyoka mkono ndipo adatigoneka kuchipatala sabata ziwiri ndi masiku 4.
Ndili konko, ndidamva kuti mwamuna wanga akuyenda ndi mnzanga, yemwenso ndi woyandikana naye nyumba. Titatuluka adabwera kudzandiuza kuti mwamuna wanga adamufunsira koma adawakana.
Nditawafunsa amuna anga adakana. Chodabwitsa nchakuti, usiku mwamuna wanga amasowa. Kuyangana kuchimbudzi, kubafa ngakhalenso pakhonde osaoneka.
Ntawapanikiza, adaulula kuti amayendadi ndi mnzangayo. Powafunsa ngati ndili ndi vuto adati palibe, koma Satana ndiye adawanyenga. Ndichitenji? EKM EKM, Amuna anuwo alibee chikondi chenicheni. Iwowo povomereza kuti amanyengana ndi mnzanu, aonetseratu ukamberembere wawo. Poyamba ndi kukana ndiye kusowa chikondiko.
Chokaikitsa china nchakuti mnzanuyo adabwera yekha kudzakuuzani kuti amuna anu adamufunsira koma adanama kuti adawakana. Ichi chidali chiphimba mmaso chabe chifukwa amadziwa kuti manongonongo a uhule wake akufikani.
Zikatere nkutani? Kunjaku kudaopsa ndipo si bwino kusekerera mwamuna kapena mkazi wosakhulupirika. Nthawi yoimbs nyimbo ya kapirire kunka iweko idatha.
Kaitureni nkhaniyi kwa ankhoswe chifukwa uwu ndi mlandu wachigololo choletsedwa ndi Ambuye.
Apachibale akundifuna Anatchereza, Pali anyamata awiri a pachibale amene akuoneka kuti amandifuna. Mmodzi mwa anyamatawo ndidamudziwa kalekale ndipo wakhala akundifundira koma ndimamukana.
Ndidadziwana ndi winayo chifukwa cha mbale wakeyo ndipo nsye akunditumizira mauthenga a chikondi, ati akundifuna. Ndichitenji, chifukwatu awiriwo akundisowetsa mtendere.
M.E.
Mponela ME, Ngati anyamatawo simukuwafunadi ndi bwino kuwauziratu, mmalo mowapatsa banga kuti aziganiza kuti mwayi ukadalipo.
Mwinatu inuyo simutsindika kukana kwanuko. Komanso nkutheka kuti anyamatawo ndi nkhakamira. Mwinanso ali pampikisano kuti aone angakutengeni ndani.
Muli monsemo, mphamvu zili mmanja mwanu, kulola kapena kukana.
Ana owapeza avuta Zikomo Anatchereza, Ndakhala pachibwenzi ndi mkazi wina yemwe ndidalowa naye mbanja chaka chatha. Iye adabwera ndi ana ake awiri ndi abale ena ndipo polingalira kuti ndi banja, nanenso ndidakatenga mwana wanga.
Iye akungokhalira kulalatira mwana wangayo ati ndi wamwano. Nthawi zina akumachita izi panja kuti a nyumba zoyandikira amve. Akuti ngakhale nditachoka sangadandaule, chonsecho ali ndi pathupi pa miyezi 7.
Ndapirira mokwanira, ndithandizeni.
WL, Lilongwe.
WL, Musanachite chilichonse pabanja mumayenera kukambirana kaye. Momwe zikuonekera apa, mkazi wanuyo adakangotenga ana ndi abale akewo musanakambirane. Nanunso mudangoyendera yanu nkukatenga mwana wanu.
Choncho kusamvana sikungalephere kubwerapo.
Komatu apa palibe chifukwa chokwanira choti nkuthetsera banja.
Khalani pansi nkumanga mfundo imodzi. Ndi ana ndi abale ati amene ayenera kuchoka pakhomopo ndipo ndi angati amene ayenera kuchoka? Mukuyembekezera mwana wanu, kusonyeza kuti udindo wanu ukukula. Anatchereza Ndimutsatirebe? Ine ndidakwatiwa ndi mwamuna wa ku Zimbabwe ndipo takhala limodzi mpaka mu 2012 pomwe adachoka kupita ku Joni. Ndili naye mwana mmodzi. Poyamba ankatumiza chithandizo ndipo timaimbirana foni koma pano olo foni saimba, chithandizonso adasiya kutumiza. Koma adandipangitsira pasipoti kuti ndimtsatire ku Joniko koma abale ake adayankhula mwathamo kuti adakwatira ku Joni komweko. Ndiye nditani pamenepa, ndikwatibwe kapena ndizidikirabe? Nditani ine, gogo wanga, poti ndidakali wachitsikana? EE, Blantyre Wokondeka EE, Ndamva nkhawa zako ndipo ndakhudzidwa kwabasi ndi mmene ukwati wako ndi mwamuna wa ku Zimbabweyo ukuyendera. Koma nanenso ndili ndi funso kuti ndithe kukuthandiza bwino. Kodi ukwati wanuwo ndi womanga bwinobwino ndipo ndi wovomerezeka ndi mbali zonse ziwiri za kuchimuna ndi kuchikazi? Ndatero chifukwa pakuoneka kuti ukwati wanu ulibe ankhoswe nchifukwa chake abale ake a mwamunayo akukuyankha mwathamo kuti uiwaleko za iye ati chifukwa adakwatira mkazi wina ku Joniko. Maukwati ambiri akhala asakulongosoka chifukwa achinyamata masiku ano amakonda madulira, osafuna kutsata ndondomeko zonse zofunikira asanalowe mbanja. Mnyamata akangoti I love you basi msungwana khosi gonekere kenaka wakamulowerera mnyumba ali basi takwatirana. Posakhalitsa mavuto otere amayamba mbanja lotereli, zinthu osalongosokanso. Tsono apa, mwana wanga, chimene ndikuona nchakuti mwamuna wakoyo walithawa banja nchifukwa chake chithandizo olo foni adasiya kukutumizira. Iwe ukamuimbira amakuyankha nanga? Ndikukaika. Likadakhala banja lenileni ndidakati upite kwa ankhoswe akuthandize, koma ndakaika ngati alipo. Ndiye chomwe ungachite apa nmumuiwala mwamunayo ndi kuyambiranso wani. Si wanena wekha kuti udakali mtsikana! Koma ulendo uno uyesetse kuti utsate ndondomeko zonse zimene zimayenera kutsatidwa munthu ukafuna kulowa mbanjaiwe ndi bwenzi lako mudziwane bwinobwino ndipo lidzaonekere kwanu ndi akwawo kudzatomera ukwati; pakhale chinkhoswe cholongosoka; kenaka ukwati wololedwa.
| 12 |
Muli mafunso mmanifesito a DPP Chipani cha DPP chatulutsa manifesito ake Lamulungu pa 7 April amene akufotokoza zomwe chipanichi chakwaniritsa mzaka zisanu zathazi komanso zomwe chipange ngati chisankhidwenso pa May 21. Zambiri zomwe DPP yasanja ndi zomwenso chidalonjeza pokonzekera chisankho cha 2014. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Chipanicho chasiya mfundo zina zomwe sichidakwaniritse mu 2014 monga kuchepetsa mphamvu za mtsogoleri wa dziko, kukozanso doko la Nsanje mwazina. Manifesito a DPP akubwera pamene chipani cha MCP ndi UTM atulutsa kale mfundo zomwe achite ngati atasankhidwa. DPP yati akangochipatsanso zaka zina zisanu, chithetseratu katangale mdziko muno ntchito yomwe ati adayamba kale kuigwira mu 2014. Pothandizira mfundoyo, DPP yati idzamanga komanso kuchotsa pa ntchito aliyense amene adzapezeke akuchita ziphuphu. Yatinso idzakhazikitsa khoti lapadera lothana ndi milandu ya katangale mfundo yomwe ilinso mmanifesito a MCP. Chipanicho chati chikapatsidwa zaka zina zisanu chidzatsitsa mtengo wa feteleza dziko lonse komanso ndondomeko ya zipangizo zotsika mtengo yomwe ilipo pano idzakhalapobe. Chatinso anthu amene alibe malo wolimapo, boma lidzawapatsa ndalama zomwe aliyense adzasankha chomwe adzachite nazo.
Chipanicho chalonjezanso kuti ntchito yomalinga nyumba zamakono kwa osauka ndi achikulire idzapitirira. Chipanicho chatinso chidzaonetsetsa kuti Amalawi ndiwo akupanga bizinesi mmidzi osati anthu obwera. Anthu akunja akuti azizapanga mabizinesi mmatauni mokha ndi mmizinda ndi mpamba wa pafupifupi US$250 000 (K185 miliyoni) womwe adzabwere nawo kuchokera kunja. Ndipo bizinesi yosaposera K50 miliyoni idzapatsidwa kwa Amalawi okha kuti apange. Chipanichi chatinso chidzaonetsetsa kuti dotolo mmodzi akuthandiza anthu 5 000 osati 33 000 monga zilili pano ndipo akuti izi zichitika mzaka zisanu zikudzazi. Msukulu zonse za ukachenjede akuti ophunzira azizagwiritsira ntchito intaneti yaulere. Mwa zina, manifesto a DPP ati mzaka zisanu zikubwerazo, chipanicho chidzapereka ndalama zokwana $3.5 biliyoni (K2.5 thililiyoni) zotukulira ntchito za mtengatenga, mphamvu za magetsi, ulimi wa mthilira, maphunziro, umoyo, zokopa alendo komanso zotumizirana mauthenga mwa njira za makono zomwe zidzapititse patsogolo chuma cha dziko lino.
Chipani cha DPP chati chidzaika pafupifupi K2.7 thililiyoni yomangira zinthu zosiyanasiyana mdziko muno kuchokera chaka cha 2019 mpaka 2024. DPP ikuti idzamanga msewu wamakono kuchokera ku Mzuzu kudutsa Lilongwe mpaka kufika ku Blantyre. Chipanicho chatinso chidzagula madesiki kwa ophunzira onse msukulu zonse mdziko muno. Koma akadaulo pa ndale ati manifesito a chipani cha DPP avuta kuwakhulupirira chifukwa zambiri zomwe akukamba ndi zomwe adalonjezanso mu 2014 ndipo chalephera kukwaniritsa. George Phiri wa ku sukulu ya Livingstonia komanso mneneri wa Malawi Political Science Association, Andrew Mpesi ati anthu sangawerenge manifesito a DPP ndi diso limodzi lokha koma kuunikiranso zomwe akwaniritsa mzaka zisanu zapitazo. Chitsanzo, mu 2014 adalonjeza kuti adzathana ndi ziphuphu, zaka zisanu zatha koma pafupifupi tsiku lililonse nyuzipepala zikuvumbulutsa katangale amene akuchitika mbomamu. Panonso akukamba zothetseratu ziphuphu ndiye mbali iyi zivuta kukhulupirira kwake, adatero Mpesi. Vuto la manifesito a chipani cholamula mkuti anthu amayangana kaye zomwe achita ndi zomwe akulonjeza, adaonjeza. Kuona kwa Phiri adati manifesito amene DPP yaphika pano sakusiyana ndi omwe idatulutsa mchaka cha 2014. Iye adati zambiri zomwe alukamo ndi zomwe alephera kukwaniritsa kuyambira mu 2014. Panopa zivuta kuwakhulupirira, kodi chinthu achilephera kukwaniritsa mzaka zisanu panopa ndiye akwanitse kuchikwaniritsa? adadabwa Phiri.
Iye adati DPP idataya mwayi kukachita nawo mtsutso chifukwa ndi womwe ukadawapatsa danga kufotokozera bwino pamene padavuta kuti akwaniritse masomphenya awo ndi momwe akwaniritsire ulendo uno. Phiri akuganizanso kuti palibe chisinthe ngati DPP ingapambane pachisankho cha pa May 21 chifukwa manifesito awo sakunena momwe adzakwaniritsire zomwe adazilephera. Ndikuona ngati manifesito a UTM ndiwo akufotokoza bwino motsatirana ndi MCP chifukwa nkhani zomwe asanja ndi zomwe anthu akukumana nazo komanso akufotokoza bwino momwe adzakwaniritsire. Mu 2014, DPP idalonjeza kuti pofika 2019 sipadzapezeka mwana akuyenda mtunda woposera makilomita kupita kusukulu zomwe sizidatheke. Chidatinso chidzapereka chitetezo kwa munthu aliyense, koma kuchokera 2014, anthu 25 achialubino aphedwa, 11 akusowa ndipo nkhani zokhudza anthuwa zafika pa 153.
Chipanichi chidatinso mzaka zisanu chidzamanga nyumba 10 000 za apolisi koma izi sizidatheke.
| 11 |
Akulimbana ndi Edzi Pothandiza kuti uthenga wokhudza matenda a EDZI ufikire achinyamata ambiri makamaka pobweretsa uthengawo pafupi ndiponso kunjira zomwe achinyamata akugwiritsa ntchito kwambiri, bungwe la Digital Multimedia Solutions ndi la Solutions ndi Sustainable Rural Growth &Development Initiative (SRGDI) lakhazikha njira yofalitsira uthengawu podzera mma CD ndi Facebook.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mkulu wa bungwe la SRGDI Maynard Nyirenda poyankhula mwapadera anati bungwe lake lakhazikitsa CD yokhala ndi uthenga wosiyanasiyana wa Edzi kuti uthenga wamatendawa ufikire achinyamata ambiri makamaka omwe ali msukulu za sekondale komwe angathe kupeza mwayi wogwiritsa ntchito computer.
Nyirenda akuti kwa omwe alibe ndi mwayi wa makinawa azipeza uthenga wofanana komanso wochulukirapo wa Edzi kudzera ku akaunti yapadera yabungweli ya Facebook.
Ngati poyambira chabe, bungwe la SRGDI likufikira sukulu makumi awiri mumzinda wa Blantyre ndi CD komanso dziko lonse kudzera pa internet.
Akatswiri a zaumoyo makamaka omwe akugwira ntchito yolimbana ndi matenda a Edzi akhala akunenetsa kuti mlili wa Edzi ungagonjetsedwe pokhapokha uthenga womveka bwino wokhuza matendawa utafikira mtundu wonse padziko lapansi.
Ngakhale izi zili zomveka bwino,kafikidwe ka uthengawu ku magulu a anthu osiyansiyana kwakhala nkovuta choncho akatswiri ena akuti zikuchititsa kuti anthu ena asapindule ndi mauthengawa.
Achinyamata apakati pa zaka khumi ndi zisanu ndi makumi awiri ndi zinayi ndi gulu lomwe mabungwe osiyanasiyana azaumoyo kuphatikizapo bungwe lazaumoyo lalikulu padziko lonse la World Health Organisation (WHO) akuti liri ndi chiwerengero chochuluka cha anthu omwe akutenga kachirombo koyambitsa matendawa tsiku ndi tsiku.
| 6 |
Alandira K14 biliyoni yotukulira maphunziro Maiko ndi mabungwe omwe amathandiza boma ati apereka thandizo la K14 biliyoni ku unduna wa zamaphunziro zotukulira maphunziro msukulu za pulayimale.
Lonjezoli lili mumgwirizano wa pakati paboma la Malawi ndi maiko a Norway ndi Germany kudzanso banki yayikulu padziko lonse ya World Bank ndi bungwe la United Nations Childrens Fund (Unicef).
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Haugen: Tiyamba chaka chino Mbali ziwirizi zidasayinirana mgwirizanowu Lachitatu pasukulu ya pulayimale ya Muzu mboma la Lilongwe ndipo oyimirira mayiko ndi mabungwewa, Kikkan Haugen, yemwe ndi kazembe wa dziko la Norway adati ndalamazi ziyamba kufika chaka chino.
Gawo loyamba libwera chaka chino ndipo lichokera ku Norway, World Bank ndi Unicef ndipo gawo lachiwiri lidzabwera 2018 ndipo lidzachokera kudziko la Germany, adatero Haugen.
Iye adatsindika kuti izi sizikutanthauza kuti maiko ndi mabungwewa ayambiranso kupereka thandizo lomwe ankapereka ku bajeti ya Malawi ndipo adasiya pa zifukwa zosayendetsa bwino ndalama za mbajeti.
Mkulu wa bungwe la mgwirizano wa mabungwe omwe amayanganira za maphunziro, Benedicto Kondowe, adati nkhaniyo ndi mayeso aakulu ku unduna wa zamaphunziro ndi boma la Malawi.
Oyendetsa pulogalamu ya thandizo la mumgwirizanowu akuyenera kuzindikira kuti tsogolo la thandizo lina mtsogolo likhala mmanja mwawo chifukwa ntchito zawo ndizo zingakope mayiko ndi mabungwe ena kuti alowererepo, adatero iye.
Nduna ya zamaphunziro ndi sayansi Emmanuel Fabiano adati boma la Malawi kudzera muunduna wake lionetsetsa kuti thandizoli labweretsa kusintha mmaphunziro a ku pulayimale mdziko muno.
Boma, sukulu ndi makolo atenga nawo mbali pachitukuko chilichonse chomwe chikhazikitsidwe mmapologalamu a mumgwirizanowu ndiponso liziyesetsa kupereka upangili ndi zofunika kuwonjerapo mmapologalamuwo, adatero iye.
| 3 |
Mvula iwononga katundu ku Phalombe Inde mvula ndi madalitso, komabe kwa anthu a ku Phalombe ndi Mulanje madalitsowa akuwalandirira kulimba.
Ngozi zogwa mwadzidzidzi zafika pena kumeneku. Mu November kudali ku Mulanje komwe anthu 500 adakhudzidwa. Pano ndi ku Phalombe komwe anthu 279 akusowa pogwira mvula ya mphepo itasasula nyumba zawo.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Wothandizira kwa wamkulu woona ngozi zogwa mwa dzidzidzi ku Phalombe Dave Chibani akuti mavutowa adayamba pa 18 December ndipo kufika pano anthuwo sadalandirebe thandizo.
Tawalembera kale anthu oyenerera kuti atithandize. Zinthu sizili bwino, kufika lero [31 December] sitidalandire thandizo lililonse, adatero Chibani.
Nako ku Mulanje anthu adakasowa pogwira. Nyumba zidasasuka ndipo anthu ena kuvulazidwa pothawira malo oti azembe ngoziyo.
Padakalipano, Chibani wati podikira thandizo, alimbikitsa kupereka mitengo kwa makomiti amene amaona ngozi zigwa mwadzidzidzi.
Mitengo 800 ndiyo yagawidwa kwa makomitiwa mboma la Phalombe mwa ma T/A 6. Mitengo imathandiza ngozi monga izi, komanso mitengoyi iwapatsa ubwino wina akabzala chifukwa ndi ya zipatso.
Sitinangowapatsa koma tinawaphunzitsa, bungwe la Concern Universal ndi bungwe la Irish Aid ndilo lidatipatsa mitengoyi kotero zitithandiza ndi ngozi yachitikayi chifukwa anthu amene tawapatsawo ndiwo amatithandiza kukachitika ngozi za dzidzidzi, adatero Chibani.
| 18 |
Kusowa kwa magazi, mankhwala ku Qech Odwala kuchipatala cha Queens amakumana ndi zokhoma Mavuto akhodzokera pachipatala cha Queen Elizabeth Central Hospital (QECH) mumzinda wa Blantyre. Kusowa kwa magazi ndi zipangizo kukuika miyoyo ya odwala pachiswe chifukwa chosowa chithandizo.
Lolemba ndi Lachiwiri pameneTamvaniidaswera pachipatalapa msabatayi idadzionera zokhoma. Imfa za anthu si nkhani yachilendo, pamene odwala ena angogonekedwa kudikirira tsiku lodzapezeka mankhwala.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Dotolo wina amene tidamupeza mchipatalachi adati vuto lakula pachipatalapa ndi kusowa kwa magazi komanso mankhwala.
Mankhwalawa ndiye sadayambe pano kusowa koma magaziwa ndiye avutitsitsa, mwina nchifukwa choti ana atsekera sukulu.
Mankhwala alipo ochepa kuyerekeza anthu amene chipatalachi chimalandira, adatero dotoloyu.
Mlembi muunduna wa zaumoyo Chris Kangombe akuti vutoli lilipo ndipo lipitirira ngati sipakhala kusintha pa ndalama zomwe undunawu umalandira.
Mndondomeko yachuma ya 2013/2014 timafunikira K28 biliyoni koma tidalandira K6 biliyoni. Timafuna mankhwala amitundu yoposa 1 000 ndiye kugula mankhwalawa kumadya ndalama zambiri. Tangoganizani tikufunikira $115 miliyoni (pafupifupi K553 biliyoni) yogulira ma ARV okha ndiye ndalama yomwe timalandira sikukwana, adatero Kangombe.
Iye adati mndondomeko ya zachuma ya 2014/15 akufuna K32 biliyoni yogulira mankhwala koma adakaika ngati ndalamayi iperekedwe yonse.
Naye mneneri wabungwe lotolera magazi la Malawi Blood Transfusion Service (MBTS) Allen Kaombe adati mavuto osowa magazi akhudza zipatala zonse mdziko muno.
Iye adati kusapereka magazi mokwanira ndiko kwachititsa kuti mavutowa akhudze zipatala mdziko muno.
Tikulephera kutolera magazi amene timawafuna omwe ndi mauniti 80 000 pachaka, mmalo mwake tikutolera mayuniti 50 000. Tikawerengetsa bwino, timayenera kutolera mayuniti 7 000 pamwezi ndi 320 patsiku. Izi sizikuchitika, tikungotolera 4 200 pamwezi ndi 190 patsiku, adatero Kaombe.
Kaamba ka mavutowa, sizikudabwitsa kumva anthu akumwalira komanso ena kusowekera pogwira mzipatala maka cha QECH chomwe tidayenderako.
Samalani ndi woyanganira odwala amene tidamupeza muwodi ya 4A. Iye amasamalira akazi ake amene amachokera mmudzi mwa Elema kwa Senior Chief Nthache mboma la Mwanza.
Iye akuti adafika pachipatalapa Lachiwiri pa 29 July mkaziyo atadwalika chifuwa chachikulu komanso kusowa kwa magazi.
Timafika pano cha mma 2 koloko usiku. Ku Mwanza timanyamuka cha mma 12 koloko matenda atakula. Chipatala cha Mwanza ndicho chatitumiza kuno chifukwa kumeneko mankhwala komanso magazi palibe, adatero mkuluyu.
Pa 29 atafika, Samalani adauzidwa kuti magazi palibe.
Iye adati: Tidasowa kopita, adatigoneka kuti tidikirire mpaka atapezeka. Pa 30, botolo limodzi lidapezeka. Litatha, adati ena sapezekanso. Takhala tikudikira ndipo ena apezeka lero [pa 5 August] koma akuti akatha ndiye angotitulutsa chifukwa kulibiretu.
Samalani akuti sipakudutsa tsiku maliro osachitika muwodi yawo zomwe zikumupatsa mantha.
Ku Mwanza tabwerako anthu awiri, anzathuwo amwalira, moti patsiku anthu awiri kapena atatu akumwalira, adatero iye.
Ngati sipakhala kusintha pa ndalama zopita ku undunawu ndiye anthu ngati Samalani akhala pavuto losasimbika.
Nchifukwa chake tikumema anthu kuti apite akapereke magazi kuti anthu otere athandizidwe, adatero Kangombe amene akuti mavuto a kusowa kwa mankhwala kwasintha poyerekeza ndi mwezi wa December wapitawo.
Naye Kaombe sakudziwa tsiku lomwe magazi ayambe kupezeka mzipatalazi. Kukhala kovuta kuti tipeze magazi chifukwa tikulephera kupeza mlingo omwe timafuna pamwezi. Mavutowa angathe tsiku lililonse ngati dziko titagwirana manja kuti tipereke magazi mwaunyinji.
Kaombe adati mavutowa akula kwambiri chifukwa ophunzira amene amapereka magazi kwambiri atsekera.
Malita 85 mwa 100 a magazi amene timatolera amachokera kwa achichepere omwe ndi azaka pakati pa 16 mpaka 25 pamene nambala yotsalayo imachokera kwa akuluakulu azaka 26 mpaka 65. Pamene sukulu zatsekera, tikuvutika kuti titolere magazi, adatero Kaombe.
| 6 |
Kalembera wa nzika wayamba Boma, kupyolera mnthambi ya National Registration Bureau (NRB), Lachitatu lidayamba gawo loyamba lolemba Amalawi kuti akhale ndi zitupa za unzika.
Gawo loyamba la kalemberayu idayamba mmaboma a Nkhotakota, Ntchisi, M chinji, Kasungu, Salima ndi Dowa. Ntchitoyi, imene ikhale mmagawo atatu, idya K36.5 biliyoni ndipo Amalawi 9 miliyoni alowa mkaundula.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Ntchito ya kalemberayo ku Mchinji Lachitatu Malinga ndi mneneri wa nthambi ya boma imene ikuyendetsa ntchitoyi ya NRB Norman Fulatira, kalemberayu wayamba bwino ndipo ndiwothandiza kwambiri.
Kukhala ndi chitupa cha unzika kuthandiza mnjira zambiri. Apolisi, akaona munthu amene akumukaikira kuti ndi wakunja, azidzamufunsa kuti aonetse chitupa chake. Polembetsa anthu opindula pa ntchito za mthandizi, sabuside, nthawi ya chisankho komanso kuchipatala, Amalawi azidzangoonetsa chitupa cha unzika, adatero Fulatira.
Fulatira adatsutsa malipoti oti pali mavuto ndi malipiro a anthu omwe akugwira ntchitoyi. Iye adati boma silidalandire lipoti lina lililonse lokhudza mavuto.
Zomwe tikudziwa nzoti malipiro adachedwa masiku awiri oyambirira okha pomwe anthuwa amachita maphunziro awo chifukwa choti tidali tikuwakonzera ziphaso, adatero Fulatira.
Pamene ntchito yopereka zitupa za unzikayo yayamba, bungwe lophunzitsa anthu zosiyanasiyana la National Initiative for Civic Education (Nice) likuthana ndi mphekesera zina zimene zingafoole Amalawi kukalembetsa.
Malinga ndi mkulu wa Nice mchigawo chapakati, anthu ena akhala akufalitsa kuti kalemberayu ndi njira yothandiza kudzabera pachisankho cha 2019.
Azipembedzo ena amauzanso anthu kuti kalemberayu akusonyeza kuti dziko likutha. Ndipo ena akuti boma likungofuna kugwiritsa ntchito kalemberayu pokapemphera thandizo kumaiko a kunja. Zonsezi ndi nkhambakamwa chabe, adatero Naphiyo.
Iye adati bungwelo lifikira Amalawi ambiri pofuna kuthana ndi mphekeserazo zimene zingasokoneze ntchito ya kalemberayo.
Mkulu wa Nice Ollen Mwalubunju adati ntchito yophunzitsa anthu za kalemberayu imavuta chifukwa madera ena adali ovuta kufika.
Kudali malo ena mmaboma a Ntchisi ndi Dowa komwe sitidafikeko chifukwa nkovuta mayendedwe. Choncho tidapempha mafumu komanso aphunzitsi kuphunzitsa anthuwa za kalemberayu, adatero Mwalubunju.
Mkuluyu adatinso agwiritsa ntchito wailesi za mmadera pofalitsa uthenga.
Iye adati bungwe lake lidakumananso ndi vuto la kusowa kwa galimoto chifukwa ntchitoyi imafuna kufikira mmadera ambiri.
Kupatula apo, Mwalubunju adatinso ophunzitsa anthuwa adakumana ndi anthu a zikhulupiro zina zomwe sizilola kulembetsa.
Koma tidawalimbikitsa kuti kalemberayu ngwa aliyense ndipo kupanda kutero kukhala kusemphana ndi malamulo a dziko lino, adatero Mwalubunju.
DC wa boma la Mchinji, Rosemary Nawasha adati mbomali mudalibe mavuto ena aliwonse pokonzekera kalemberayu.
| 11 |
Ambuye Msusa Apempha Anthu Akalembetse Mkaundula wa Voti Mwaunyinji Arkiepiskopi wa arkidayosizi ya Blantyre, Ambuye Thomas Luke Msusa alimbikitsa akhristu amu arkidayosiziyi kuti atenge nawo gawo pa chisankho cha pulezidenti chatsopano chomwe chikuyembekezeka kuchitika pa 2 July chaka chino.
Ambuye Msusa, anena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi.
Aliyense amene wafika msinkhu wovota akalembetse-Msusa Iwo ati ndi kofunika kuti anthu akalembetse mu kaundula wa voti ndi cholinga choti adzavote ndi kudzasankha mtsogoleri wakumtima kwawo yemwe adzatsogolere dziko lino zaka zisanu zomwe zikudzazi.
Aliyense amene wakwanitsa zaka 18 akuyenera akalembetse ndi kudzavota pa tsiku la chisankho. Amene tinalembetsa kale tipitenso tikawone ngati dzina lathu lilipobe mkaundulayu, anatero Ambuye Msusa.
Arkiepiskopiyu wapemphanso achinyamata omwe amatenga gawo pa ntchito yokopa anthu kuti achite izi molemekeza ufulu wa ena.
Iwo anati, Nthawi yokopa anthu, ena amakhala ndi mantha komanso amavutika chifukwa achinyamata ena amachita chipongwe posalemekeza maganizo a anzawo, kusalemekeza katundu wa anthu ena mpaka kuwabera ngakhalenso kupha anzathu.
| 11 |
Mutharika asankha nduna Pangotha maola sipikala wa Nyumba ya Malamulo Richard Msowoya atagwirizana ndi atsogoleri a zipani za mNyumba ya Malamulo kuti asankhe komiti yoti iziyendetsa zochitika mNyumbamo kaamba ka kusowa kwa nduna, mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika adasankha nduna zina mbandakucha wa Lachinayi.
Zinthu zidaima mNyumbayo Lachitatu pomwe aphungu adasowa chochita chifukwa komiti yomwe imasankha nkhani zimene aphungu akambirane patsiku padalibe. Komitiyo imayenera kukhala ndi wapampando yemwe ndi nduna ya boma.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Msowoya adaimitsa msonkhano wa aphunguwo kuti ayambenso kukambirana 9:30 Lachinayi koma pomwe kumacha nkuti Mutharika atasankha nduna zatsopano 9 zimene zidalumbiritsidwa cha mma 8.
Mwa ndunazi, amayi ndi awiri: Dr Jean Kalirani, amene ndi nduna ya zaumoyo komanso nduna ya zamasewero, achinyamata ndi chikhalidwe Grace Obama Chiumia. Chiumia ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa aphungu a kumbali ya boma.
Ndipo nduna 6 nzochokera mchigawo cha Kumwera, ziwiri za Pakati pomwe ziwiri, tikaphatikizapo nduna ya zachuma Goodall Gondwe yemwe adali woyambirira kusankhidwa nduna, ndi za Kumpoto.
Samuel Tembenu, yemwe ndi nduna ya zalamulo ndi nduna yokhayo imene si phungu. Iye adalephera kupeza mpando wauphungu ndi mavoti ochepa kwambiri mdera la pakati ku Salima. Izi zikusonyeza kuti Mutharika wasankha nduna ziwiri zomwe si aphungu chifukwa nduna ya zachuma Goodall Gondwe amene adasankhidwa pampandowo mmbuyomu adalephera kupeza mpando wa uphungu kumpoto mboma la Mzimba.
Nduna ya zamtengatenga ndi Francis Kasaila, amene adalephera kukhala sipikala wa Nyumba ya Malamulo atagonja kwa Msowoya Lolemba, pomwe nduna ya zofalitsa nkhani ndi Kondwani Nakhumwa. Nduna ya zaulimi ndi Dr Allan Chiyembekeza, yemwe adali wapampando wa komiti ya zaulimi mNyumba ya Malamulo ya pakati pa 2009 ndi 2014.
Henry Mussa, amene ndi mkulu wa aphungu a boma mNyumbayo ndi nduna ya zantchito, pomwe Emmanuel Fabiano, amene adakhalapo mkulu wa sukulu ya ukachenjede ya Polytechnic, ndi nduna ya maphunziro. George Chaponda ndi nduna yoona za maiko akunja.
Izi zikusonyeza kuti boma la Mutharika tsopano likuyendetsedwa ndi anthu 12, kuphatikiza mtsogoleri wa dziko linoyu ndi wachiwiri wake Saulos Chilima. Mwandunazi, zisanu zidakhalapo nduna mboma la mkulu wake wa mtsogoleri wa dziko Bingu.
Mkulu wa bungwe loona kuti maphunziro ndi apamwamba la Civil Society Education Coalition Benedicto Kondowe adati kusankha nduna zambiri zochokera dera limodzi kungachititse kuti madera ena asapindule.
Ndunazi zikhoza kumakondera madera awo pachitukuko, choncho madera ena angamve kuwawa ndi ulamulirowu, adatero Kondowe.
Ndipo mmodzi mwa akadaulo pa ndale Mustafa Hussein adati ambiri mwa omwe adasankhidwawo, ena adali mu ulamuliro Bingu.
| 11 |
Mantha pa Wenela Titakhala pamalo aja timakonda pa Wenela, adafika gogo wina. Iye adavala nkhope yachisoni.
Ana inu, mwataya chikhalidwe. Mwalowerera kuba, kupha ndi kuononga. Inu, a satana oyenda ndi mapazi, adatero gogo uja.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Tonse tidadabwa kuti nkhaniyo imayambiranso pati.
Bwanjinso, gogo? Chavutanso nchiyani? adafunsa Abiti Patuma.
Ndinu alendo kodi pano pa Wenela kuti simunamve za kuphedwa kwachitika masiku apitawa? Wophedwayotu adakaponyedwa pafupi ndi nyumba ija munkakhala Mfumu Mose, adafotokoza gogoyo.
Abale anzanga, pa Wenela paterera. Kukacha, nkhani za kuba mbweee! Kuphana ndiye kudya kwa awa ndi awo.
Palibetu chimene chikuyenda. Mwinatu tingolimbikira ufiti chifukwa njala nayo ndi iyi ili pakhomopo, adatero gogo uja.
Chaka chinonso galu wakuda adutsa? Abale tidyenso mapira, mchewere ndi nyika? adafunsa Abiti Patuma.
Anthu ayamba kale kudya zimenezo. Simunalowere ku Nsanje pakatipa? ndidafunsa.
Apa Gervazzio adaika nyimbo ina yake: Lili kuti lili kuti mnzanga dziko lija Lomwe ana ankangothawa Kuthawa njoka osati munthu.
Masiku amakedzana, makwangwala akuikira pansi, kudalibe kuphana umu mukuchitira leromu. Kodi mwalowa chiwanda chotani mmitima mwanumo? Inde mudzithemba u-mafia koma dziwani nthawi imakwana, adatero gogo uja.
Chifukwa chokoledwa ndi nkhani zachisoni zidayala nthenje pa Wenela, Abiti Patuma adati tilowere ku sitediyamu, chifukwa kudali mpira. Ndidavomera monyinyirika chifukwatu kubwalo la masewera limeneli tsopano kwalowa mphepo ina. Mukukumbukira wina adafako miyezi yapitayo. Mwakumbukanso ena adavulala tsiku lokumbukira kuti pa Wenela timadzilamulira tokha ife ojiya, osenza ndi osolola, sitilabada za British Overseas Main Administration imene idamanga goli tate, mayi ndi ana awo.
Mukumbukatu bwino tsiku lija Moya Pete adathawa anzake awiri ati kukafuna kuchezetsa abale ena mtauni.
Zidali ngati kholo loitana mnzake kuchisangalalo chakuti mwana wake wakwanitsa zaka 51. Mnzakeyo atabwera pakhomopo, tate wa mwanayo nkumamutsanzika kuti akupita mtauni ndipo mlendo akhoza kumaonera kanema, adatiuza Abiti Patuma.
Musamutero Moya Pete. Ndikumvatu kuti adachoka mpira uli mkati chifukwa anali atatopa zedi. Komansotu paja akuti amakonda kugona osati masewero, adatero Gervazzio.
Nchifukwa chaketu ndimaona ngati ndi bwino akadati munthu wotenga mpando wa Mfumu Mose asamadutse zaka 60. Lero taonani mkulu wa zaka 90 akuyanganira anyamata othamanga magazi a zaka zosaposa 60 amene akhoza kumupusitsa kuti achoke pakhomo patafika alendo, adatero gogo uja.
Zoona adamuuza kuti sakhala woyamba chifukwa gogo uja adapeza Tadeyo asanavale zovala kwawo kwa Kanduku naye sankamaliza kuonera mpira wadolola, adatero Abiti Patuma.
Titafika kubwalo la masewero, tidalandiridwa ndi utsi wokhetsa misozi.
Koma masewero tadana nawo chiyani. Onani apolisi awo akuombera uyo, uyo, uyo! Tikabisala kuti? ndidalira.
Abale anzanga, tivomereze kuti pano pa Wenela zinthu zatilaka. Mwina tilimbikire ufiti, uthakati basi.
| 7 |
UDF ibalalika ku Nyumba ya Malamulo Mpungwepungwe udabuka mu Nyumba ya Malamulo yomwe idatsegulidwa Lolemba pomwe aphungu a chipani cha United Democratic Front (UDF) adaonetsa kusamvana pankhani yonkhudza mbali imene azikhala munyumbayi.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Pomwe msonkhano wa aphunguwo umayamba, aphungu a UDF adakhala mbali yotsutsa koma mawa lake adakhamukira mbali ya boma.
Lachitatu pomwe tinkalemba nkhaniyi nkuti mlembi wamkulu wa chipanichi Kandi Padambo atatsindika kuti mbali yokhazikika yomwe aphungu awo azikhala siinadziwike chifukwa akuluakulu achipanichi akadali mkati mokambirana.
Tikadakambirana za nkhaniyi ndiye sindinganene kuti aphungu athu azikhala mbali iti mpaka zopingapinga zonse zitatha, adatero Padambo.
Mpungwepungwewu udayamba nyumbayi isanatsegulidwe pomwe komiti yakale ya chipanichi idalemba kalata kwa Sipikala wa nyumbayi Henry Chimunthu Banda kupempha kuti aphungu awo apatsidwe malo mbali yotsutsa.
Ganizoli lidasinthidwa ndi komiti yatsopano yachipanichi yomwe idalemba kalata ina kwa sipikalayu kupempha kuti aphungu awo abwerere kumbali ya boma koma tsiku lotsegulira nyumbayi Lolemba, wokhazikitsa bata mu UDF, Clement Chiwaya, adalemba kalata ina yopempha sipikala kuti aphungu onse achipanicho apite mbali yotsutsa.
Lachiwiri, aphungu a UDF anachedwa kulowa mnyumbayi ndipo pobwera, Chiwaya anabweretsa kalata ina kwa sipikala yomwe imapemphanso kuti aphungu a UDF abwerere mbali ya boma.
Sipikala wa nyumbayi Henry Chimunthu Banda adatsimikiza kuti adalandiradi makalata osiyanasiyana kuchokera ku chipanichi okhudza mbali yomwe aphungu ake azikhala mnyumbayi.
Lero lomwe ndalandira kalata ina kuchokera ku chipanichi kuti ganizo lawo loyamba lija lasintha ndipo akufuna kubwerera kumbali ya boma, adatero Banda atangolandira kalata yachitatu yokhudza nkhaniyi mnyumbayi.
Mpungwepungwewu uli mkati, aphungu ena 12 omwe adachoka muchipani cha Democratic Progressive Party (DPP) kulowa chipani cha Peoples (PP) adalengeza kuti abwerera mchipani chawo chakale.
Nayenso phungu wa dera la kumadzulo ku Mchinji Theresa Mwale walengeza kuti wachoka kumbali ya boma ndipo padakali pano ndi phungu oima payekha koma aphunguwa akana kunena zifukwa zomwe akuchokela mu chipani cha PP.
Nyumbayo ikuyembekezera kukambirana nkhani yokhudza chisankho cha magawo atatu chomwe chikuyembekezeka mu 2014.
| 11 |
Fodya wobwerera kumsika amugulitsa Mkulu wa bungwe la Tobacco Association of Malawi (Tama), Graham Kunimba, wati fodya yemwe anabwerera pamsika chaka chino tsopano amugulitsa.
Iye adati ngakhale zinthu zinavuta, bungwelo lidayesetsa kukambirana ndi boma, bungwe la Tobacco Control Commission (TCC) ndi ogula kufikira tsopano fodya yense amugulitsa. Mwa magawo 100 alionse a fodya wofika kumsika, 70 akhala akubwezedwa chaka chino, ndipo alimi ambiri manja anali mkhosi kusowa chochita naye.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Alimi a fodya ngati uyu ayenera kukhala ndi zitupa Kunimba wati malonda a fodya mchakachi anavuta kwambiri chifukwa fodya analimidwa wochuluka kwambiri kuposa mlingo omwe ogula amafuna. Kafukufuku akusonyeza kuti dziko la Malawi limayenera kulima fodya okwana makilogalamu 158.1 miliyoni koma chaka chino tinakolola makilogalamu 205.53 miliyoni.
Ngakhale fodyayu amugula, mitengo yake inali yotsika kwambiri. Izi zapangitsa kuti dziko lino lipeze ndalama zochepa ku ulimiwu kusiyana ndi chaka chatha. Kafukufuku akusonyeza kuti chaka chatha dziko la Malawi lidapeza K216.8 biliyoni kuchokera ku fodya, koma chaka chino tapeza K162.6 biliyoni.
Pamenepa ndiye kuti boma lapeza ndalama zochepa komanso msonkho wochokera ku ulimiwu wachepa ndipo mwachidziwikire chuma cha boma chakhunzidwa, adatero Kunimba.
Mkulu wa bungwe la Farmers Union of Malawi (FUM), Alfred Kapichira-Banda, wavomereza za kugulitsidwa kwa fodyayu ndipo adati fodyayu amugula mongolanda. Fodya wambiri amugula pamtengo wa K553 pa kilogalamu ndipo wina amugula kuchepera apo, adatero Kapichira-Banda.
Mmodzi mwa alimi omwe anakhudzidwa ndi vutoli, Isack Banda wa mboma la Dowa, wati zomwe wakumana nazo mchakachi zayamba kumupatsa maganizo osiya ulimiwu chifukwa sanapeze phindu lililonse.
Ulimi wa fodya umalowa zambiri komanso umalira zipangizo zochuluka ndi zokwera mtengo moti ndikawerengetsa zonsezi palibe chimene ndaphula koposa ndingoleka, adatero Banda.
Bungwe la Tama likuchenjeza kuti mlimi amene sanalandire chilolezo kuchokera ku TCC asalime fodya chifukwa sadzagulidwa kumsika.
Bungweli lati izi zithandiza kuti fodya yemwe alimidwe chaka chino asapyole mlingo omwe dziko la Malawi likuyenera kulima. Kunimba adati alimi omwe alandira chilolezochi apatsidwa mlingo wa fodya yemwe akuyenera kulima.
Tikuwalangiza alimi onse kuti asatire mlingo omwe TCC yawapatsa ndipo asapyole, kuopa kuchulutsa zokolola zomwe zingapangitse kuti malonda adzavutenso chaka chamawachi, adatero Kunimba.
| 2 |
Anthu Atsopano Alowa DPP ku Mangochi Chipani cha Democratic Progressive (DPP) chati chikukula mchigawo chakumvuma kaamba ka zitukuko zomwe chikuchita mchigawochi.
Gavanala wa chipanichi mchigawo chakumvuma kwa dziko lino, Julius Paipi wanena izi lolemba pa msonkhano womwe anachititsa pa sukulu ya pulaimale ya Namalaka mdera la Lutende mboma la Mangochi komwe amalandira mamembala atsopano a mderalo ochoka ku chipani cha Peoples kulowa mchipani cha DPP.
Zimenezi zikutanthauza kuti anthu akukhutitsidwa ndi ulamuliro wa chipani cha DPP chifukwa cha zitukuko zomwe chikuchita mdziko muno. Ife ndi onyadira kwambiri.
Ngati kunatsala dera lomwe PP inali ndi mphamvu ndiye dera lake ndi limeneli koma zimenezi zikutanthauza kuti tayimaliza Mangochi yonse ndipo ndi ya DPP basi, anatero Paipi.
Iye wati kulowa kwa anthu mchipanichi kukusonyeza chikhulupiliro chomwe anthu ali nacho mwa chipanichi malinga ndi ntchito za chitukuko zomwe chikugwira.
Khwimbi la anthu pa msonkhanowo Polankhulapo yemwe anali wapampando wa chipani cha Peoples mdera la Mangochi Lutende, Yatima William anati achita izi atawona kuti deralo likutsalira pa nkhani za chitukuko kaamba kosankha aphungu a mbali yotsutsa boma.
Anthu amene anditsatira ine ndi oposa 7000 ndipo tachita zimenezi chifukwa dera lathu likutsalira kwambiri pa chitukuko ndiye tawona kuti bola tithawire ku mbali ya boma kuti dera lathu litukuke msanga kusiyana ndi kukhala kumbuyo kwa otsutsa, anatero William.
| 11 |
Wobwerera lili pululu amwaliranso ku zomba ZImene zachitika mmudzi mwa Makoloni kwa T/A Mwambo ku Zomba masiku apitawa nzoda mutu. Mayi wa zaka 28 amene adabwerera kumanda sabata ziwiri zapitazo bokosi la maliro lomwe adagoneka mtembo wake litayamba kunjenjemera, wamwaliranso atangokhala kwa masiku anayi.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Mfumu ya mmudzimo komanso woyandikana nyumba atsimikizira Msangulutso Lachiwiri lapitali za malodzawa ndipo ati anthu mmudziwo akuganiza kuti zachitikazi nzamasalamusi.
Wojambula wathu kufanizira ndi mmene zidakhalira tsiku limene Tamara Faliji adauka kwa akufa Patrick Matemba, yemwe adaona zododometsazi zikuchitika, adauza Msangulutso kuti Tamara Faliji adagwa kunyumba kwake masana a pa 11 August.
Sitikudziwa chomwe chidachitika koma adangogwa. Tidamutengera kuchipatala cha Makwapala Health Centre komwe adatiuza kuti wamwalira, adatero Matemba.
Monica Mbewe, namwino wa pachipatalachi yemwe adatsimikiza za imfayo poyamba, adauza Msangulutso kuti zomwe wodwalayo amaonetsa zidasonyeza kuti wamwalira.
Adafika ali ndi moyo ndipo ndidayamba kumupatsa thandizo. Patatha mphindi 30 ndidaitanidwanso ndi amene amamuyanganirawo kuti ndikaone zomwe akuchita. Panthawiyo amaonetsa zizindikiro zoti wawalira.
Pamtima sipamagunda, thupi lidangolobdoka, diripi ya madzi ndi mankhwala idasiya kuyenda. Apa zidasonyeza kuti wamwalira moti ndineyo ndidalembera kuti wamwalira, adatero namwinoyu.
Nyakwawa Makoloni potsimikiza za nkhaniyi, idati itamva za malirowo, idalamula anthu kuti ayambe kukonzekera zoika maliro mawa lake.
Mawa lake adzukulu adakumba manda ndipo anthu a mmudzimu adakhoma bokosi. Mwambo wa maliro utatha tidanyamula zovuta, ulendo kumanda, idatero mfumuyi.
Koma Makoloni adati anthu adadabwa kuona bokosi likugwedera atangofika kumanda.
Apa nkuti mwambo wakumandako utangoyamba kuti titsitsire bokosi mmanda ndipo ndidalamula kuti bokosilo litsekulidwe.
Titatsekula tidaona kuti wakufayo akutuluka thukuta komanso amadziwongolawongola, adatero Makoloni.
Iye adati mwambo udathera panjira ndipo adakwirira dzenje la mandalo nabwerera ndi woukayo kunyumba komwe kudaitanidwa ampingo wina wa Pentecost kuti amupempherere.
Pakulowa kwa tsikulo, akuti mayiyo adakwanitsa kudya phala koma movutikirabe.
Amangovumata, kuti ameze ndiye kudali kovuta, komabe adadya pangono, adatero Matemba.
Kulankhula ndiye adasiyiratu ndipo pamasiku onsewo amangodya phala. Pa 16 August adadzuka wolefuka ndipo adasiya kudya. Kenaka mpamene timamva kuti wamwaliranso.
Tidakhulupirira kuti ulendowu adamwaliradi chifukwa mkhwapa mudali mutazizira ndipo samatulukanso thukuta. Tidakaika maliro pa 17 August, adatero Makoloni.
Koma mfumuyi yati ikuganiza kuti zomwe zidachitikazo zidali zamasalamusi ndipo akukhulupirira kuti imfa ya mayiyo wina adaikapo dzanja.
Chilowereni ufumu zotere sindidazionepo. Ineyotu ndikuti ndidali pomwepo ndipo ndidadzionera zonsezi zikuchitika. Ndinadabwa nazo ndipo ndikukaika kuti zotere zingangochitika; alipo amene akukhudzidwa kuti mpaka mayiyu afe imfa yotere, idatsindika mfumuyi.
Akuti malirowo atangochitika, adzukulu ndi anthu ena adamenya gogo ake a womwalirayo pomuganizira kuti akukhudzidwa ndi imfa yachilendoyo.
| 19 |
Kolondoloza: Mwambo wokaona mwana wa Inkosi Kumayambiriro kwa chaka chino Angoni ochokera mboma la Mzimba adali chimwemwe tsaya kaamba ka kubadwa kwa mwana wamwamuna kubanja lachifumu la Inkosi ya Makhosi Mmbelwa ku Edingeni mboma la Mzimba. Mwa mwambo wa Angoni, mwanayu ndiye akuyembekezereka kudzalowa ufumuwu mtsogolo muno. MARTHA CHIRAMBO adacheza ndi Ndabazake Thole, mlembi wamkulu wa bungwe la Mzimba Heritage, yemwe akulongosola za momwe mwambowu udayendera motere: Ndakupezani wawa, ndamvetsedwa kuti mudapita kokaona mphatso ku Edingeni. Talongosolani, kodi mwambowu umayenda bwanji? Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Poyamba ndinene kuti koyambirira kwa chaka chino ife Angoni tidasangalala kwambiri ndi kubadwa kwa mwana wa mwamuna kwa Inkosi ya Makhosi Mmbelwa. Paja ufumu wa Agonifetu timaupitiriza ndi kubadwa kwa mwana wamwamuna kubanja lachifumu. Zikatero timakhala ndi chikhulupiriro chonse kuti ufumu upitirira ndipo timapemphera mwamphamvu kuti Mulungu amuteteze mwanayu.
Zikomo wawa, pitirizani kulongosola za mwambowu tsopano.
Mwanayu atabadwa, uthenga udatumizidwa kwa makhosi onse kapena nditi mafumu onse Achingoni ku Ekwendeni, Elangeni ndinso ku Emucisweni komanso midzi ina yonse. Uthengawu udatipezanso ife.
Mutalandira uthenga mudachitapo chani? Ife tidayamba kutsata ndondomeko yake yoti tikaone mwanayu. Sikuti umangodzuka lero ndi lero basi ndikukaona mwana, ayi, sititero. Ulendo wathu udali ndi zolinga zitatu monga kukamuona mwanayu, kukadziwa dzina lake, komanso kukapereka mphatso. Tidapempha kudzera kwa Inkosi Mpherembe yomwe ndi mlembi wamkulu wa khonsolo ya mafumu mwa a Mmbelwa. Kupatula apo, tidapemphanso kwa nduna ya komwe kulikulu ku Edingeni yomwe idatiloleza. Tidabwereranso kwa Mpherembe kukapemphanso chilolezo.
Nthawi yokaona mwana itakwana zidatani? Adatipatsa Inkosikazi Mtwalo kuti ndiyo itsogorere ulendowu. Pajatu ntchito yokaona mwana imaimira kwambiri azimayinu. Mwa ichi pagulu lathu abambo tidalipo ochepa kulekana ndi amayi.
Mwakambapo zokapereka mphatso. Mudanyamula mphatso zanji? Azimayi adatenga ufa, shuga ndi zina ndi zina zokhudza mwana, pomwe ife madoda tidanyamula kandiwo kake. Tidatenga mbuzi ngati ndiwo. Nanga ufa umayenda wopanda ndiwo zake? Tsopano mutafika ku Edingeni, mudayambira pati? Ife ngati madoda tidapereka malonje. Koma sitidakambeko kalikonse zokhudza kuona mwana. Pajatu tati ntchitoyi eniake enieni ndi amayi. Inkosikazi ndiyo idafotokoza cholinga cha ulendowo womwe tidapita a Mzimba Heritage ochokera ku Mzuzu, Mzimba boma komanso ku Lilongwe. Apa tidapereka mphatso.
Mudapereka mwana musadamuone? Talongosolani bwino pamenepa.
Iyo idali ya malonje chabe chifukwa ife Angoni tisadamuone mwana uja pamakhala mboni. Iyi ndi ndalama yomwe timaika mmbale yosonyeza kuti mtima wathudi tikufunitsitsa timuone mwanayu. Ndipo posakhalitsa amayi ndi agogo ake aakazi a mwana adatutuluka naye. Komatu tonse sitidamugwire kupatula inkosikazi chifukwa uyu ndi mwana wachifumu.
Zonsezi zimachitika musadadziwebe dzina? Eya. Udali mwambo wopatsa chidwitu ndi wosangalatsa kwambiri. Tidaperekanso mboni ina kuti tidziwe dzina ndipo makolo ake adatiuza kuti ndi Londisizwe lomwe likutanthauza mtetezi wa dziko kapena kuti mvikiliri wa charo mChitumbuka. Atangotchula dzina azimayi adalulutira komanso kuvina, ndipo ife a bungwe tidayamba tsopano kutumiza mauthenga palamya komanso paintaneti kwa abale ndi abwenzi za dzina. Dzina la mwana wa Inkosi ya Makhosi sumangouzidwa basi; pamakhala mboni ngati momwe zidachitikiramo.
Kodi akadabadwa mwana wamkazi chisangalalo chikadakhala chimodzimodzi? Pachikhalidwe chathu, akakhala mwana wamkazi zimapereka maganizo ndithu kwa anthu poganizira kuti ufumuwu salowa ndi munthu wamkazi. Koma akakhala mtsikana timadziwa kuti tsiku lina adzakwatiwa ndipo adzachoka pamudzi.
| 1 |
Kugwiririra ana kudzatha? Pafupufupi tsiku lililonse tikumamva kapena kuwerenga malipoti akuti mwana wagwiririridwa penapake.
Omangidwa akumangidwa. Kugwira ndende ndiye kosakamba koma zikuoneka kuti zilango zomwe zinaikidwa kwa ogwirira anthu zikulephera kuthetsa mchitidwewu.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Kuphatikiza apo, pali zilango zina zoti anthuwa akapatsidwa iwe wakumva umagwa nazo mphwayi kapena kukhumudwa kumene.
Malamulo a dziko lino amati chilango chokulitsitsa kwa munthu wogwiririra mwana wochepera zaka 14 ndi kukakhala kundede moyo wake wonse pamene wopezeka wolakwa pongofuna kugwiririra mwana, amayenera kukakhala kundende zaka 14.
Ngakhale malamulowa ali chonchi, pali ena oti akagwiririra mwana amangopatsidwa ndede ya zaka zitatu kapena zisanu.
Ngakhale makhoti ali ndi mphamvu zosiyana pakaperekedwe ka chilango, pakuyenera kupezeka njira ina yoonetsetsa kuti ogwiririra ana apatsidwe ndende yowawa.
Zilango zingonozingonozi zapeputsa nkhanza yogwiririra ana ndipo zikulephera kuopseza ena ofuna kugwiririra ana.
Mwachitsanzo, wina akauzidwa ndi singanga kuti chizimba chopezera chuma ndi kugwiririra mwana, nkwapafupi munthuyu kupirira ndende ya zaka zisanu chifukwa aziti ndikatuluka kundede ndidzasambira mchuma choposa.
Koma kugwiririridwa ndi chipsinjo chosaiwalika kwa olakwiridwa ndipo ena amatha kusokonekera mutu kumene.
Nchifukwa chake maiko ena amaika dongosolo loti anthu ochitiridwa nkhanzayi athandizidwe ndi akatakwe a momwe munthu amaganizira kuti moyo wawo usasokonekere.
Izi ndi zina zomwe unduna ndi mabungwe oona za ana angamaganizireko kuchita pambali powerengetsa ana amene akuchitiridwa nkhanza zamtunduwu.
Koma koposetsa malingaliro alunjike popeza njira zoti munthu aziopera kutalitali kukhudza mwana mosayenera.
Njira yapafupi ndiyo kukhwimitsa chilango kwa ogwiririra ana powapatsa ndende ya moyo wonse kapenanso kuwadula ziwalo zimene akuononga nazo miyoyo ya ana osalakwa.
| 7 |
Boma Lathetsa Quota System, Kubwenzeretsa JCE Boma lalengeza kuti labwenzeretsa mayeso a JC komanso lathetsa ndondomeko yosankhira ophunzira kupita ku sukulu za ukachenjede yotchedwa Quota System.
Walengeza za kusinthaku-Susuwele Banda Nduna ya zamaphunziro Dr. William Susuwele Banda ndi yemwe walengeza izi pa msonkhano wa atolankhani omwe unachitika lero masanawa mu mzinda wa Lilongwe.
Ndunayi yati izi zikutanthauza kuti mayeso a JCE ayamba kulembedwa chaka cha maphunziro cha 2020-2021 ndipo ophunzira adzayamba kulembanso mayesowa chaka chamawa cha 2021.
Boma lakhala likutsatira mwachidwi ndemanga za anthu osiyanasiyana. Komanso ophunzira ambiri akhala akulephera mayeso awo a MSCE kaamba koti amatayilira komanso akakhala zaka zinayi ndi kulephera mayseo a fomu 4 amakhala kuti alibe chilichonse choti awonetse chosonyeza kuti anapita ku sekondale, anatero a Banda.
Koma polankhulapo katswiri pa zamaphunziro Dr. Steve Shara wati ngakhale ndondomekozi zili ndi kuthekera kosintha momwe ntchito za maphunziro ziziyendera mdziko muno, pakufunika kuti boma ndi magawo onse okhudzidwa agwirane manja pothana ndi mavuto omwe akubweretsa mbuyo maphunziro mdziko muno monga kusowa kwa zipangizo zophunzitsira komanso kuphunzilira.
| 3 |
Siteshoni ya Nkaya ifewetsa maulendo Gawo lachiwiri lomanga siteshoni ya sitima ya Nkaya mboma la Balaka layamba ndipo ntchitoyi ikuyembekezeka kutha mu November chaka chino.
Mneneri wa bungwe loona sitima zapamtunda la Central East African Railways (CEAR) Chisomo Mwamadi wati gawoli likatha, anthu amene amagwiritsira ntchito sitima zapamtunda athandizika chifukwa sitima zizinyamula katundu wambiri komanso ziziyenda mwachangu.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Mwamadi: Samalani njanji Mu June chaka chino, bungweli lidamaliza gawo loyamba lomwe kudali kumanga njanji zinayi kuti sitima zapamtunda zizidutsana pamalopa.
Gawo lachiwiri lidayamba litangotha gawo loyamba lomwe kukhale kumanga njanji ina yotalika ndi makilomita awiri komanso kumanga njanji zinayi zomwe zizithandiza kusungirako sitima komanso kumasula mabogi.
Njanji zimenezi ndizomwe tizimasulira sitima ngati ili ndi vuto komanso kusungirako sitima. Pamene tikupanga izi, sitima zina zizitha kumayenda mopanda kusokonezedwa. Izi sizimachitika poyamba chifukwa tidalibe malo, koma tsopano izi ziyamba kuchitika popanda vuto lililonse, adatero Mwamadi.
Padakali pano, malo amene amangepo njanjizi asalazidwa kale komanso katundu wafika kuti ntchitoyi iyambe tsiku lililonse.
Njanji yopita ku Nkaya ndi imeneyi Mwamadi akuti gawoli likatha, anthu amene amagwiritsira ntchito sitima asangalala kwambiri komanso bizinesi izichitika mwachangu.
Zonse zikatha, ndiye kuti Nkaya akhala malo akulu pomwe sitima zizisemphana komanso kumamangirira mabogi. Sitima yochokera ku Mwanza, Blantyre, Liwonde komanso Kanengo zizidutsana pa Nkaya komanso titha kumamanga mabogi.
| 2 |
Miyezi inayi idutsa mafumu osalandira mswahala Nyakwawa komanso magulupu akudandaula kuti matumba awo abooka kaamba koti patha miyezi inayi asakulandira mswahala.
T/A Nthache wa ku Mwanza wati kusalandira mswahalaku kwakhudza ntchito zachitukuko kumeneko chifukwa mafumuwa sakutumiza anthu kuti akagwire ntchito zachitukuko monga kulambula misewu ndi zina.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mafumuwa adzandidandaulira. Ndikawaitana kuti tikagwire ntchitozi zikuvuta, sakutumiza anthu awo zomwe zikuchedwetsa ntchito zambiri zaachitukuko, adatero Nthache.
Koma nduna ya za maboma aangono, Grace Maseko, wati izi sakudzidziwa chifukwa mafumu onse adalandira ndalama zonse zomwe zidatsala mu December chaka chatha.
Ngati pali ndalama zomwe sizidaperekedwe ndi za mwezi wa March basi, adatero Maseko.
Iye adatinso boma lidasintha momwe mafumuwa angalandirire ndalama zawo. Poyamba timawaikira kubanki koma pano amalandira pamanja pa 27 mwezi ulionse, adatero Maseko.
Koma malinga ndi mafumuwa, zomwe akunena Maseko ndi njerengo.
Nyakwawa Mussa ya kwa STA Amidu kwa T/A Kalembo mboma la Balaka akuti kumeneko akhala akufunsa kwa omwe amabweretsa malipiro awo koma palibe amalongosola chomwe chikuchitika.
Sizili bwino, ngakhale malipiro athu ndi ochepa, tikuyenera kulandira, adatero Mussa.
Gulupu Kapochi wa kwa T/A Zilakoma mboma la Nkhata Bay wati kumenekonso malipirowa sadalandire kwa miyezi inayi.
Ntchito zachitukuko tayimika kaye kuti tifufuze za malipiro athu. Tidakagwada kwa gogocharo koma nawonso akuti sakudziwa zomwe zikuchititsa kuti tisamalandire malipiro athu. Tikupempha boma litithandize, adatero Kapochi.
Mafumu enanso a ku Balaka ndi Ntcheu omwe adati tisawatchule maina, adatsimikiza za nkhaniyi ndipo ati palibe chifukwa chomalimbikira ntchito zakumudzi chikhalirecho sakulandira malipiro awo.
Muulamuliro wa DPP, malemu Bingu wa Mutharika adati mafumuwa azikalandirira ndalama kubanki kuti afanane ndi ogwira ntchito mboma.
Izi zidasinthadi. Mafumu adayamba kulandirira malipirowo kubanki kusiya njira yomakalandirira kwa DC. Njirayi mafumuwa, maka magulupu ndi nyakwawa, adaidandaula ponena kuti akuyenda mtunda wautali koma kukatenga malipiro ochepa. Iwo adati malipirowo akungothera kukwerera basi kapena matola.
Chaka chatha mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda, adalamula kuti mafumuwa ayambenso kulandira pamanja. Chisinthireni, mafumuwa akhala akudandaula kuti malipiro akumachedwa.
Padakalipano, magulupu akulandira K5 000 pomwe nyakwawa ndi K2 500 pamwezi.
Mafumu ena akhala akudandaula kuti malipirowa akuchepa ndipo boma liwaonjezere chifukwa zinthu zakwera kutsatira kugwa kwa ndalama ya kwacha.
Ogwira ntchito mboma ndi ena adakwezeredwa malipiro awo koma mafumuwa sadaone kusintha.
| 8 |
Joyce Banda Wauza Anthu Aku Zomba Avotere Chakwera Mtsogoleri wakale wa dziko lino yemwenso ndi mtsogoleri wa chipani cha PP, Dr. Joyce Banda wapempha anthu mdziko muno kuti akavotere Dr. Lazarus Chakwera pa chisankho cha mpresident chomwe chikudzachi kuti dziko lino lisinthe pa chuma.
Banda: Dziko lino likufunika atsgoleri owopa Mulungu Dr. Banda amayankhula izi lero ku Chinamwali mu mzinda wa Zomba pa msonkhano wotsiriza okopa anthu omwe anachititsa mogwirizana ndi mlangizi wa chipani cha UTM a Noel Masangwi. Iwo ati anthu oyenera kulamulira mdziko lino akuyenera akhale owopa Mulungu monga a Chakwera komanso a Chilima.
Ndimafuna kuwona wachichepere kuposa ine, osadakwa, owopa Mulungu ndiye ine nnawapeza omwe ndakuonetsani apa a Chakwera ndi a Chilima kuti tidzaone feteleza otchipa komanso nyumba mmidzimu, anatero mayi Banda.
Mmawu ake mlangizi wa chipani cha UTM, a Noel Masangwi anati chipani cha DPP chakonza upandu woti chipatse DC wa boma lililonse ndalama zokwana 2.5 million kwacha kuti abele chisankho chomwe chikudzachi.
Lachiwiri Minister of Local Government a Ben Phiri anapita ku MRA kuti akapange budget kuti atenge 2.5 million ampatse DC aliyense kuti abere chisankhochi, anatero a Masangwi.
| 11 |
Anthu Awiri Afa Atagwera Mu Mtsinje ku Rumphi Anthu awiri omwe ndi a Nathaniel Gondwe a zaka 35 zakubadwa komanso a Hotters Mhango a zaka 15 zakubadwa afa atagwera mu mtsinje wa Lunyina mboma la Rumphi pomwe amaweza nsomba mu mtsinjemo.
Wachiwiri kwa wofalitsa nkhani za apolisi mbomalo Sergeant Tupeliwe Kabwilo watsimikiza zangozi-yi.
Iye wati anthuwo amaweza nsomba ndipo anafa chifukwa cha kubanika.
Athuwo amaweza nsomba mu nsinje wa Lunyina ndipo atamaliza kuwezako Hotters anagwera mmadzimo ndipo Nathaniel amakampulumutsa koma mwasoka nayenso anamira, anatero Sergeant Kabwilo.
Padakalipano apolisi akulangiza anthu a mderalo kuti apewe kuwoloka mitsinje yakuya kuopa ngozi zamtunduwu.
| 14 |
Chipatala cha boma chitsekedwa loweruka Miyoyo ya anthu pafupifupi 50 000 ozungulira chipatala cha Mkanda Health Centre mboma la Mchinji imaikidwa pachiopsezo Loweruka chifukwa sichitsekulidwa patsikulo mosemphana ndi dongosolo la unduna wa zaumoyo.
Mneneri wa unduna wa zaumoyo Adrian Chikumbe adauza Msangulutso Lolemba kuti chipatalacho chimayenera kutsekulidwa ndi Loweruka lomwekuchoka mmawa mpaka nthawi ya nkhomaliro. Kuposera apo, madotolo amayenera kusamala odwalika zedi kapena a matenda obwera mwadzidzidzi.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Ngakhale izi zili choncho, chipatalachi chimalandiranso odwala kuchokera mzipatala zina zazingonozingono 5, omwe akafika pamalopa Pachiweru, amakhala kakasi.
Kafukufuku wathu wasonyeza kuti chipatalachi sichimatsekulidwa Loweruka chifukwa mkulu woyanganira pamalopa, yemwe sitimutchula dzina, amapemphera tsikulo.
Ndipo kusatsekulidwa kwa chipatalachi kukuchititsa ena mwa anthu ofuna thandizo kupita kuzipatala zomwe si zaboma kapenanso chipatala cha Tamanda chomwe chili mdziko la Zambia.
Bambo wina, yemwe adakana kutchulidwa dzina, adati mwana wake wa zaka 12 amene adafika naye pachipatalapo kumapeto kwa 2015 adamwalira kaamba kosowa chisamaliro. Iye adati adapita ndi mwanayo akuonetsa zizindikiro za malungo Lachisanu nthawi itadutsa 11 koloko usiku koma dotolo adakana kuwathandiza usikuwo.
Adakana kudzuka ndipo patadutsa maola awiri mwanayo adamwalira. Apa tidapempha mlonda kuti akawauze kuti mwanayo watisiya ndipo atithandize koma adangomuuza kuti tizipita kumudzi, adatero bamboyo, Wina mwa okhudzidwa ndi vutoli, yemwe ndi mphunzitsi pa sukulu ya sekondale mderalo, adati wabwererapo kawiri konse mchaka chathachi pachipatalachi.
Ulendo wina, mwezi wa October, ndidabwerera ndi mwana wanga wa zaka zitatu yemwe amadwala mphumu. Chifuwachi chitakwera cha mma 7 koloko usiku wa Loweruka, ndidathamangira kuchipatala komwe ndidapezako anthu ena awiri odwala akudikirira, adatero iye.
Iye adaonjeza kuti atabwera mkulu wa pachipatalapo, adawanyengerera kuti awathandize ndipo adangowalembera enawo kuti azipita chipatala cha kuboma.
Koma mwana wanga adakanitsitsa kumulemba mpaka adatibweza, adatero munthuyo yemwe wakana kutchulidwa dzina.
Iye adapita kuchipatala cholipira komwe adalipira K4 500.
Mkulu wa komiti ya kayendetsedwe ka chipatalacho ya health advisory committee (HAC) Thomas Bisiketi adatsimikiza kuti odwala saonedwa patsikulo ndipo mbali ya amayi obereka yokha ndi yomwe imakhala ikugwira ntchito.
Mkulu wachipatalapo sagwira ntchito patsikuli, koma ife ngati a HAC timaoona ngati ndi momwe zipatala zonse zaboma satsegula Loweruka, adatero Bisiketi.
Malinga ndi wapampando wa komiti ya chitukuko kwa mderali Anorld Chitedze, chipatalachi chakhala chisakutsekula Pachiweru kwa zaka zitatu tsopano.
Iye adati chipatalachi chili ndi ogwira ntchito asanu okha, omwe atatu aiwo ndi anamwino, ndipo awiri ndi olembera odwala.
Mkulu wachipatalachi amatiyankha kuti amapita kutchalitchi Pachiweru ndipo chipatala satsekula. Koma ife timadabwa kuti bwanji sauza ena omutsata kuti azithandiza anthu patsikulo? adatero iye.
Popheramphongo, Mfumu yaikulu Mkanda idati kafukufuku wake wasonyeza kuti chipatalachi sichitsekulidwa Pachiweru ndipo odwala ochokera mzipatala zazingono zozungulira deralo monga Kazyozyo, Kaligwazanga ndi Gumba, amawapatsa bedi podikira Lolemba.
Odwala akabwera Lachisanu, samawaona tsiku lomwelo. Iwowa amapatsidwa bedi mpaka Lolemba. Sitikudziwa kuti nkutani. Chaka chatha tidapempha kuti atichotsere, koma tangodabwa kuti wagoneranso. Pano nzeru zatha, idatero mfumuyo.
Iyo idati masiku ena mkuluyo amatha kungothandiza owadziwa kapena munthu akamkomera mtima.
Iye adati nkhaniyi idakafika ku likulu kwa bomalo ndipo adamkhazikako bwalo pamaso pa akuluakulu a boma ndi dotolo wamkulu wa bomalo yemwe pano adasamukira ku boma lina.
| 6 |
Anatchezera Za Chikondi ndi chibwenzi Agogo, Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Kodi chibwenzi ndi chikondi ndi zosiyana bwanji? Mwina funso limeneli likhoza kuoneka ngati lopanda nzeru koma kwa ine ndi lofunika kwambiri. Funso lina ndi loti kodi ngati mwamuna amakonda kulonjeza chibwenzi kapena wachikondi kuti adzakwatirana chonsecho mkazi samamulonjeza mwamuna wake, ndiye pamenepa mwamuna angathe kupitiriza chibwenzi kapena angomusiya? LF, Area 12, Lilongwe Wokondeka LF, Munthu utha kukhala ndi abwenzi ambirimbiri koma wachikondi mmodzi. Nthawi zambiri anthu satha kusiyanitsa pakati pa chikondi ndi chibwenzi. Chikondi ndi chozama kuposa chibwenzi; chikondi chimachoka pansi pa mtima ndipo nthawi zambiri anthu awiri akakondana maka pakati pa mwamuna ndi mkazi amagwirizana mzambiri moti nchifukwa chake mapeto ake amalolerana ndi kulumbira kuti adzakhala limodzi mpaka moyo wawo wonse mbanja, pamene chibwenzi mumatha kugwirizana pa zina koma kusiyana mzambiri zochitika. Nchifukwa chake munthu utha kukhala ndi abwenzi ambiri ngakhale uli pabanja, monga ndanena kale, koma amene umatherana naye nkhazi zakukhosi ndi zakumphasa ndi mmodzi yekha, wachikondi wako. Funso lako lachiwiri yankho ndi loti pachikhalidwe chathu mwamuna ndiye amafunsira mkazi ndipo ndi iyeyo amene amauza mkazi za cholinga chake pachibwenzi chawocho. Akazi ambiri amakhala ndi manyazi kunena kuti alola chibwenzi chonsecho mkati mwa mtima wawo alola kale. Ndiye munthu wamwamuna uyenera kumvetsa ndi kufatsa; osapupuluma chifukwa ukhoza kutsekereza mafulufute kuuna poganiza kuti mkazi sakunena chilichonse. Pamene pali chikondi sipasowa, zochitika zimasonyeza zokha kuti apa pali chikondi ngakhale wina asanene.
| 12 |
Zipolowe zikuphulika Pamene tikuyandikira chaka cha 2014 pomwe Amalawi akuyembekeza chisankho cha magawo atatu chosankha Pulezidenti, aphungu a Kunyumba Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC ya Malamulo ndi makhansala, bungwe loona momwe zinthu zikuyendera mdziko muno la (PAC) lati mchitidwe wa zipolowe pakati pa zipani ukhoza kusokoneza zokonzekera chisankhochi.
Wofalitsa nkhani za bungweli mbusa Maurice Munthali wati ngati chipani chikutchuka ndi mchitidwe wamtopola komanso ziwawa, anthu omwe amafuna kudzachisankha amatha kukhumudwa ndi kusintha maganizo.
Iye watinso zipani zikachulutsa ziwawa zimachepetsa mwayi wawo wodzigulitsa kwa anthu omwe akanazisankha.
Anthu amafika pozolowera kuti chipani chakuti chimakonda zipolowe ndiye chikakhala ndi msonkhano anthu amaopa kupitako chifukwa cha mbiri yoipayo, chipani nkumalephera kudzigulitsa, adatero Munthali pocheza ndi Tamvani sabata ino.
Munthali watinso nthawi zambiri atsogoleli a zipani ndiwo amapangitsa kuti anthu owatsatira azikonda ziwawa makamaka chifukwa cha kalankhulidwe komaso zochita zawo ndipo wati izi zikhoza kutha pokhapokha atsogoleri atamvetsetsa tanthauzo la ndale.
Vuto ndi lakuti atsogoleli a zipani samvetsetsa tanthauzo la ndale. Mmalo moti azitenga atsogoleri anzawo a zipani zina ngati opikisana nawo, amawatenga ngati adani awo zomwe zimawapangitsa kuti azilankhula mtopola. Udani wotere umalowelera mwa otsatira zipani omwe amati akakumana amangokhala ngati anayambana kale basi ndewu nkuyambira pomwepo, watero Munthali.
Wachiwiri kwa mneneri wa apolisi mdziko muno, Kelvin Maigwa, wati panthawi ino yomwe chisankho chikuyandikira, apolisi akhwimitsa chitetezo ndipo salekerera munthu aliyese yemwe apezeke akuyambitsa ziwawa.
Sitiona kuti ndi ndale kapena ayi. Ntchito yathu ndi kuonetsetsa kuti pali bata ndi mtendere ndiye munthu aliyese yemwe apezeke akuchita kapena kuyambitsa ziwawa adzamangidwa, watero Maigwa.
Zipani za ndale zati pakadalipano zili kalikiriki kuphunzitsa ozitsatira ake, makamaka achinyamata, kupewa zipolowe ndipo zati zipitiriza ntchitoyi mpaka chisankho chidzachitike chaka chamawa.
lino Jolly Kalelo, mneneri wa chipani cha Malawi Congress Party (MCP) chomwe chikuyembekeza kupanga msonkhano wake waukulu wokasankha maudindo mawa lino, wati chipanichi chili ndi nthambi yoona za achinyamata yomwe imaphunzitsa achinyamatawo za makhalidwe abwino.
Ife timakhulupirira kuti boma sungatenge chifukwa chomenya anzako ayi, koma kupanga mfundo zabwino zoti anthu akhutire nazo. Pachifukwa ichi timaphunzitsa achinyamata athu za mtima wodzichepetsa ndi kumvetsa, watero Kalelo.
Wolankhulira chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) Nicholas Dausi wati ziwawa zikhoza kuchepa pandale ngati mchitidwe wonyozana ndi kutukwanana pamisonkhano ungathe chifukwa ndiwo umayambitsa maphokoso.
Vuto lalikulu limakhala zolankhula za atsogoleli pamisonkhano chifukwa ngati akuima pansanja ndi kuyamba kutukwana anzawo, anzawowo sangasangalale nazo ndipo mapeto ake ndi nkhondo. Chofunika kwambiri ndi kuona zomwe atsogolelife timalankhula pagulu, tikatero achinyamata ndi otitsatira athu sangapange ziwawa ayi, watero Dausi.
Mchitidwe wa zipolowe pakati pa zipani udayamba kalekale koma zaoneka kuti mchitidwewu wawonjeza pano pomwe nyengo ya chisankho ikuyandikira.
Bungwe loona kuti achinyamata akupatsidwa mphamvu zokwanira komanso kuwaphunzitsa mmene angatengerepo mbali pa zitukuko zosiyanasiyana la Youth Empowerment and Civic Education (Yece) lati kwa nthawi yaitali lakhala likuphunzitsa achinyamata kuipa kolowerera mikangano ya ndale.
Akuluakulu a ndale amati akayambana amanyengerera achinyamata ndi katundu kapena ndalama kuti akathane ndi adani awowo mapeto ake achinyamatawo ndiamene amamangidwa kapena kuvulala ndiye ife takhala tikuwaphunzitsa kuwopsa kwa mchitidwewu moti tili ndi chikhulupiliro kuti pakhala kusintha, watelo mkulu oyendetsa bungwe la YECE Lucky Mbewe.
Sabata yatha zipani za United Democratic Front (UDF) ndi Peoples Party (PP) zidasemphana zochita ku Zomba pomwe odzaimira chipanichi cha UDF pachisankho, Atupele Muluzi, ankakapangitsa msonkhano wa ndale pasukulu ya Mponda.
Mneneri wa polisi ku Zombako, Thomeck Nyaude, adauza nyuzipepala ya The Nation kuti mkanganowo udayamba anthu omwe adavala zovala za chipani cha PP atazungulira kumalo a msonkhanowo pagalimoto ndipo otsatira chipani cha UDF sadakondwe ndi zomwe adachita anzawozo.
Izi zidachitika patangotha sabata ziwiri wotsatira chipani cha PP Jimmy Phiri adakhapidwa ndi otsatira chipani cha DPP ku Nancholi mumzinda wa Blantyre.
Pomwe chipani cha DPP chimakonzekera msonkhano wake waukulu, anthu ena amene akuwaganizira kuti ndiwotsatira Peter Mutharika adakaotcha katundu wina wa Frank Julius, yemwe amati amatsatira yemwe amapikisana ndi Mutharika, Henry Chimunthu-Banda.
Zipani ziwirizi zidalimbanaso mwezi wa January ku Balaka komwe anthu ena adavulazidwa kwambiri otsatira chipani cha UDF atadzudzula otsatira chipani cha PP kuti adawazulira mbendera.
| 15 |
Sitalaka pa Wenela Lidali Lachinayi usiku ndipo tidali malo aja timakonda pa Wenela kukambirana izi ndi izo. Adachuluka adali madilaivala ndi makondakitala a minibasi.
Ife ojiya, osenza ndi osolola tidalipo ochepa.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Apapa afune asafune, mawa kulibe woyendetsa minibasi kuchoka pano pa Wenela, adayamba nkhani mmodzi mwa madalaivala.
Komatu tikanaganiza kale. Mawalo msuzi tikaupeza kuti? adafunsa kondakitala wina.
Koma akanadziwa! Anzakewo adamuukira, kumuthira maphuzo, monga achitira anthuwa pamsewu! Nkhani yavuta ndi ya msuziyo! Mabwana aja akamangala papolisipa kuti akatigwira tizilipira ndife osati mabwanawo. Msuzi uzikwaniranso apapa? adafunsa wina bata litabwerera.
Koma inuyo chikuvuta nchiyani makamaka kuti zifike apa? adafunsa Abiti Patuma.
Kodi ndiwe mlendo? Apolisi ayamba kugwiritsa ntchito malamulo amene akutipweteka kwambiri. Sitikufuna zimenezo, adatero wina.
Kodi malamulowo ali mmabuku? adafunsanso Abiti Patuma.
Kodi ukufuna kuvuta bwanji? Kapena ndi zibwenzi zako? Malamulowo ndi wokhazikika kungoti samawagwiritsa ntchito ndiye pano akufuna kutifinya, adayankha mkulu wina, mmaso muli gwaaa! Komatu tinzeru tikucheperako apapa. Ndikuona kuti mutichedwetsa nazo. Tsono mukayamba kuchita zionetsero zokwiya ndi malamulo okhazikika, simukuona kuti masiku akubwerawa nawo ogwiririra adzachita zionetsero kuti chilango cha zaka 14 kwa opezeka olakwa chakula kwambiri? adaponya funso lina Abiti Patuma.
Onse adangoti duuu! Ngati malamulo mukuona kuti akhwima kwambiri, mukadakambirana ndi aphungu anu kuti akasinthitse izi ku Nyumba ya Malamulo. Wina akhoza kubwerapo ndi Minibus Regulations Bill. Osati zanu za umbuli mukuchita apazi, adapitiriza.
Palibe, kaya wina afune kaya asafune, ife tikukachita zionetsero basi, adatero wina, akutulutsa chikwanje.
Adachinola pamsewu.
Mawa lake ndiye kudali moto. Ndidaona anthu akuyenda wapansi kuchoka ku Ndirande mpaka mtauni. Ochokera ku Machinjiri adali kukwera malole. Ku Manja ndi Chimwankhunda ndiye tidamva za kuphwanyidwa kwa galimoto zina. Eyi! Eyi Eyiiiiii! Posafuna kutsalira, zigandanga za ku Machinjiri zidaotcha khoti chaka chatha zidathira moto maofesi apolisi atatu. Ati kusafuna kumangidwa.
Pomwe moto umazilala Loweruka, madalaivala aja adagwirizana zokweza mtengo wa minibasi.
Abiti Patuma adati ndimuperekeze ku Queens. Pa Mibawa, adati mtengo wakwera kuchokera pa K200 kufika pa K250.
Chifukwa? adafunsa.
Kaya, adayankha kondakitala.
Abiti Patuma adalipira K500 ya anthu awiri. Kenaka adatangwanika pa WhatsApp. Sindikudziwa ankalemba chiyani, koma uthenga womaliza udali woti: Tikumana pachipatala pasiteji.
Titafika pasitejipo, tidapeza kuti amalankhula ndi anzake awiri.
Kwerani ndalipira kale kuchoka mu Blantyre ya anthu awiri. Asakulipiritseninso ameneyu. Akachita makani, manambala aapolisi aja si nkhani. Anthu ogenda kupolisi chamba chili mthumba awa, adatero Abiti Patuma.
| 7 |
Kulandira mwana ndi nkanulo Zikhulupiriro zina ukamva, mutu wake weniweni sowe. Pali zambiri zomwe makolo amakhulupilira paumoyo wa munthu kuyambira kubadwa mpaka kumwalira. Anthu ena akuti amakhulupirira kuti mwana akabadwa, pamafunika mwambo wa nkanulo ati kusonyeza kuti mwanayo walandiridwadi pakati pa abale. STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi mayi Miriam Chongwe a kwa mfumu yaikulu (T/A) Maganga mboma la Salima yemwe akufotokoza zambiri za mwambowu.
Mayi Chongwe (kumanja) kulongosola za mwambo wa nkanulo Mayi, ndati ndicheze nanu pa mwambo wa nkanulo. Mwambowu ndi wotani? Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Uwu ndi mwambo womwe umatsatidwa mwana akabadwa kusonyeza kuti abale ndi anthu pamudzipo amulandira ndipo ndi mmodzi wa iwo. Izi zimatanthauza kuti ndi mfulu kukhala ndi malo monga muja zikhalira ndi malo a banja chifukwa munthu wongobwera amavutika kupeza malo chifukwa palibe mizu yake yomwe angalondoloze.
Mwambowu umayenda bwanji? Sikuti anthu amachita kusonkhana ngati momwe miyambo ina imakhalira, ayi. Chomwe chimachitika nchakuti mwana akabadwa, chinthu choyambirira nkudziwitsa abale, makamaka amalume ake kapena azakhali, omwe amakanena kwa amfumu kenako anthu amamasuka kupita kukaona mwanayo ndi kumupititsira mphatso ngati ali nazo.
Mukati chinthu choyambirira mukutanthauzanji poti azaumoyo amati mwana akangobadwa, pompo ayamwe? Zimenezo nzoona koma apa tikukamba za mwambo. Umu ndimo makolo kalelo ankakhulupirira zinthu zisadayambe kusintha. Masiku ano miyambo yambiri ikutha pangonopangono chifukwa cha maphunziro, anthu adayamba kuzindikira kuti miyambo ina imaononga mmalo mokonza zinthu.
Tsopano mukati nkanulo timadziwa tanthauzo lokanula koma apapa pali mgwirizano wanji ndi mwambo? Eya, ndimayembekezera funso limenelo. Kumbukani kuti ndati chimakhala chinthu choyambirira mwana akangobadwa ndiye kukanulako nkutsegula mwanayo kukamwa kuti akhoza kuyamwa chifukwa walandiridwa pakati pa mudzi ndi banja lomwe wabadwiralo.
Inu mudachitapo mwambo umenewu? Mzaka za mmbuyomo nditangokwatiwa kumene koma kenako ndidazindikira kuti nkulakwa chifukwa chimakhala chilango kwa mwana. Mwachitsanzo, kumatheka kuti panthawi yomwe mwana wabadwa, palibe mayendedwe achangu malingana nkuti nthawiyo mauthenga amachita kukaperekedwa pakamwa kapena pakalata, foni kudalibe nthawi imeneyo ndiye mudikire munthu ayende kukapereka uthenga kuno mwana ali ndi njala.
Koma madotolo ndi anamwino amadziwa kuti izi zikuchitika? Sindikudziwa koma zimachitika kwambiri chifukwa chochirira kwa azamba mmidzi. Mwina ndinene kuti kukhwefula ntchito za azamba ammidzi kudathandiza nawo kuchepetsa mwambo umenewu. Sindikukhulupirira kuti dotolo kapena namwino angalekerere izi zikuchitika.
Pano zinthu zili motani? Panopa zinthu zili bwino chifukwa ndi maphunziro a zauchembere wabwino, anthu tidatsekuka mmaso. Mwina pena ndi pena zikhoza kumachitikabe poti uthenga umafika mosiyanasiyana koma nkhani yaikulu ndi yoti anthu ambiri adatsekuka mmaso chifukwa olo zokachirira kwa azamba ammidzi zidachepa.
| 15 |
Chekucheku kuno ayi Chekucheku: Sindichoka ufumu mpaka nditafa Chigamulo pamwamba pa chigamulo. Patangotha sabata imodzi bwalo lalikulu lamilandu mumzinda wa Blantyre litabwezeretsa T/A Chekucheku wa mboma la Neno pampando, anthu ena mbomali ati sakugwirizana ndi chigamulo cha bwalolo kotero achitanso zionetsero zoonetsa mkwiyo wawo.
Chekucheku, yemwe dzina lenileni ndi Francis Magombo, adaimitsidwa ndi pulezidenti wopuma Joyce Banda pa 15 May 2014 koma mtsogoleriyo sadapereke zifukwa zomuimitsira kugwira ntchito yake ngati T/A.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Kalata yoimitsa mfumuyi idati: Malinga ndi mphamvu zopatsidwa kwa ine pamutu 23:03 ndime II gawo 11 (2) la malamulo okhudza mafumu, ndikuimitsa inu Francis Magombo kuti musagwirenso ntchito za ufumuwu mboma la Neno kuyambira tsopano mpaka zofufuza zokhudza magwiridwe anu a ntchito zitatha.
Koma mfumuyi idathamangira kubwalo la milandu kuthemba kalatayo ndipo malinga ndi zomwe Chekucheku adauza bwalolo, Banda adamuimitsa chifukwa amalola zipani zonse kuchititsa misonkhano ya ndale mdera lake.
Yemwe amaimira mfumuyi pamlanduwo, Golden Mbeya, adati Chekucheku amayenera auzidwe mlandu womwe adapalamula. Izi mkalata ya Banda mudalibe.
Malinga ndi chigamulo cha bwalo ndiye kuti mfumuyi yayambiranso kugwira ntchito yake ya ufumu mboma la Neno, zomwe zakwiyitsa anthu ena kumeneko amene aopseza kuti achita zionetsero.
Anthu oposa 200 pa 2 April mpaka pa 3 chaka chino adachita zionetsero zokakamiza DC wa bomalo, Memory Kaleso Monpeiro, kuti achotse mfumuyi.
Monpeiro adatsimikiza kuti ofesi yake idalandira kalata ya madandaulowa ndipo adatumiza zodandaula za anthuwo ku ofesi ya pulezidenti.
Monga mukudziwa kuti nkhani zochotsa mfumu zili mmanja mwa pulezidenti ndiye ndidazitumiza kwa oyenera, adatero Kaleso Monpeiro.
Ofesi yake akuti sidagwire ntchito kwa masiku awiri anthuwo atatchinga ndi mitengo ndipo adaopseza kuti achokapo pokhapokha mfumuyi ichotsedwe pampando.
Mmodzi wa anthuwo, yemwenso akuyankhulira gululo, Steve Donda, wa mmudzi mwa Donda, adati mfumuyi yakhala ikulanda minda ya anthu.
Ikumadyetsera ngombe zake mminda mwathu, zomwe zikuononga mbewu zathu, komanso ikulonga mafumu posatsata ndondomeko ya ufumu wa Chingoni. Anthu amene akuwalowetsa ufumu si angoni, adatero Donda pouza Tamvani msabatayi.
Pano akuti anthuwa ayambiranso zionetsero mpaka mfumuyi itachotsedwa. Donda wati chigamulocho sichidawakomere.
Sitikufuna kuti mfumuyi itilamulirenso. Ngati akufuna kuti akhale mfumu ndiye kuno ayi, apite kwina. Tikumana, ndipo tikatsekanso ofesi ya DC mpaka mfumu imeneyi ichotsedwe, adatero Donda.
Koma Chekucheku akutsutsa zomwe anthuwa akunena ndipo akuti akukhulupirira kuti akumuchitira kaduka chabe.
Ndi zabodza kuti ndikumatsegulira ngombe ndi kukazidyetsa mminda mwawo ndipo zoti ndikulonga mafumu mosatsata chikhalidwe cha Chingoni komanso ponena kuti mafumuwo si Angoni ndi bodza.
Ndine Mngoni ndipo ndinenso ndidalimbikitsa chikhalidwechi mbomali. Sindichoka pampando wa ufumu mpaka nditafa, adamenyetsa nkhwangwa pamwala motero Chekuchechu.
Polankhulapo pa za kufunika kwa mafumu, katswiri wa zandale, Henry Chingaipe, akuti mafumu ndi ofunika ndipo dziko lino silidafike pomagwira ntchito yake popanda mafumu.
Iye akuti chofunika nkuti dziko lino lifotokozenso bwino ntchito ya mafumu ndi mtsogoleri wa dziko kuti pasakhale mpungwepungwe wa momwe mafumu amagwirira ntchito.
Malamulo okhudza mafumu [Chiefs Act] adapangidwa nthawi ya chipani chimodzi koma malamulo omwewa akugwira ntchito pamene tili ndi zipani zambiri. Chofunika nkuti malamulowa akonzedwenso kuti tidziwe ntchito zawo komanso momwe pulezidenti angagwirire ntchito ndi mafumuwa, adatero Chingaipe.
Iye adati malo ambiri ali mmanja mwa mafumu, zomwe nzovuta kuti mafumu achotsedwe pamene nkhani za malamulowa sizidalongosoke.
| 8 |
Amayi Alindi Ufulu Opititsa Patsogolo Ntchito Zampingo-CCJP Wolemba: Glory Kondowe Bungwe la chilungamo ndi mtendere mu dayosizi ya Dedza lati amayi alindi udindo opititsa patsogolo ntchito za mpingo wakatolika.
A Kasudze omwe ndi modzi wa akulu abungweli mu dayosizi ya Dedza powonjezerapo ati kafukufuku yemwe bungwe lawo lachilungamo ndi mtendere lachita akusonyeza kuti amayi ambiri sakutenga nawo gawo pogwira ntchito zikulu-zikulu zomwe mpingo wakatolika umalimbikitsa maka posapezeka mmaudindo akulu-akulu, komaso kupereka maganizo ku ntchito zomwe mpingo ukugwira.
Mwazina a Kasudze anati akhazikitsa magulu omwe azigwira ma parish awiri a Kasina komanso Bembeke kuti azimayi azikhala pansi kukambirana mavuto omwe amayi akukumana nawo.
Ndi zomwe kafukufuku umene tapedza zoti amayi azikhala nawo pampando komanso amayi akumachitilidwa nkhaza zosiyanasiyana zomwe zimawapangitsa kubwedzeretsa moyo wawo wachikhristu, anatero a Kasudze.
Padakalipano amayiwa apatsidwa maphunziro oyenera kuti aziwawunikira muzikhomo zomwe akudutsamo monga za Gender Equality Act.
| 13 |
Timakaonera masewero a mpira Masewero a pakati pa Police Secondary School ndi St Paul Private Secondary ku Zomba adzakhala chikumbutso kwa Owen Chaima, kuti adapezerapo nyenyezi yomwe lero wamangitsa nayo woyera.
Zoti masewerowo adatha bwanji, Owen sakumbukanso chifukwa chomwe amakumbukira bwino ndi Talandila Mwandira amene pakutha pa masewero adapeza chisangalalo, lero njoleyi ikugonera pachifukwa chake.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Nganganga mpaka imfa: Owen ndi Talandira Umotu mudali mu 2008 pamene Owen, yemwe ndi goloboyi wa timu ya mpira wamiyendo ya Mbeya City mdziko la Tanzania adaona dzanja la Mulungu.
Tonse timakonda masewero ampira, patsikuli tidangopita kukaonera mpira. Basitu kukumana kwake kudali komweko, adatero Owen.
Pamene masewerowo amachitika, nkhani zosaleka zidali zikukambidwa ndipo maso pa masewerowo adachoka pamene chidwi chidali pa ubwenzi umene Owen amafuna uyambike. Komabe Talandira adali asadachilandire kuti avomere.
Pakutha pa masiku chibwenzi chidayamba ndipo nkhani zatsogolo zidayamba kuphikidwa.
Inetu mwamunayu ndidamukonda chifukwa cha khalidwe lake lodzichepetsa komaso ndimadziwa kuti adali Mulungu amene adatilumikizitsa, adatero Talandira yemwe lero ndi mayi Chaima.
Pa 11 November sabata yapitayo, awiriwa adalumbira ku Mount Oliver CCAP ya ku Chilobwe mumzinda wa Blantyre kuti mpaka imfa ndiyo idzawalekanitse ponenetsa kuti kusowa kapena kupeza zachepa kufika powalekanitsa.
Mwambowu udafika penipeni pamene awiriwa adatengera unyinji wa anthu ku Miracle Garden ukutu ndi ku Naperi mumzindawu komwe kudali kumwelera ndi kudya tofewa.
| 16 |
Adzinjata Kaamba Ka Mkazi Wamwini Chisoni chidaphetsa nkhwali. Ku Masasa, mumzinda wa Mzuzu mnyamata yemwe adalembedwa ntchito ya zomangamanga pakhomo pa bambo wina mderali mongomuthandiza atamumvera chisoni kaamba ka kuvutika, akumuganizira kuti adapezeka akuzemberana ndi mkazi wa njondayo.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Koma zachisoni-nkhaniyi akuti yatengera Joseph Nyirongo, yemwe adali wa zaka 23, kumanda atapezeka ali lende mumtengo wa paini pambuyo pomupezerera akuchita zadama mnyumba mwake ndi mkazi wa njondayo.
Nyamhone: Nachi chitsa cha mtengo wotembereredwa, pomwe adadzimangirira mwana wanga Wachiwiri kwa mneneri wa polisi mchigawo cha kumpoto, Cecilia Mfune, watsimikiza za nkhaniyi.
Mkati mwa sabatayi Msangulutso udacheza ndi mwini mkaziyo, Lovemore Luhanga, yemwe adanenetsa wamukhululukira atchalitchi atamukhazika pansi ndipo wati samusiya mkazi wake.
Luhanga, yemwe amaoneka mosatekeseka ndi mbiri yomwe yatchuka mderali, adati zili kwa mkazi wakeyu kusintha kapena ayi ati kaamba koti zomwe adachita zapangitsa munthu wina kuluza moyo wake.
Koma pachikhalidwe ndiwatumiza kaye kumudzi kuti akapitidwe mphepo yabwino; adzachita kubweranso, Luhanga adatero.
Bamboyu adati panthawi yodzikhwezayo Nyirongo adali atavala scumba ya akazi ake ya mtundu pepo (purple).
Mwana wanga wa zaka zitatu ndiye adaizindikira scumbayo chifukwa adapita ndi mnzake wa zaka 8 kukaona thupilo lili mumtengo ndipo adayamba kulozera mnzakeyo kuti amvekere amama bafwa, bali muchikhuni ataona scumbayo, Luhanga adatero.
Polongosola chomwe chidatsitsa dzaye, iye adati adayamba kumva mphekesera kuti mkazi wake akuzemberana ndi mnyamatayu mwezi wa November chaka chatha.
Luhanga, yemwe amachita bizinesi komanso ndi diraiva wa lole, adati mkazi wake wakhala akukana za chibwenzichi.
Amati sangachite naye chibwenzi chifukwa Nyirongo sankasamba; ndipo nanenso ndimakaikira chifukwadi adalibe ukhondo, iye adatero.
Koma Luhanga adati chibwenzichi chitafumbira, mkazi wakeyu adamupezera nyumba mnyamatayo komanso adayamba kumamupatsa ndalama zomwe amakatolera kubizinesi yawo yoperekera sopo wochapira ndi mafuta odzola.
Bamboyu adati Lachiwiri sabata yapitayo adalimba mtima ndi kumufunsa Nyirongo za mphekeserazo, zomwe ati mnyamatayo adakanitsitsa kwa mtu wa galu kuti sakudziwapo kanthu.
Apa akazi anga adatulukira ndipo nawonso adakanitsitsa za nkhaniyi. Ndidangowauza kuti ngati akuchitadi izi, tsiku la fote lidzawakwanira ndipo chomwe chitadzachitike sindidzalankhula zambiri. Tili mkati mokamba mayi anga adatulukira kudzatichezera ndipo nkhaniyi idathera pomwepo, adafotokoza motero Luhanga.
Iye adati patadutsa nthawi adatengana ndi mkazi wake komanso mwana wawo wa zaka zitatu kuwaperekeza mayi ake; koma mwadzidzidzi adazindikira kuti mkazi wake sali nawo paulendowu ndipo sikudziwika komwe alowera.
Luhanga adati adachoka koperekeza mayi ake nthawi ili cha mma 9 koloko usiku adatsekera ana mnyumba ndi kuyamba kufufuza komwe mkazi wakeyo adalowera chifukwa adali ndi K43 000 yomwe adatolera tsiku limenelo.
Iye adati nthawi ili cha mma 1 koloko mmawa anthu ena adamutsina khutu kuti mkazi wakeyo akamuyangane kunyumba kwa Nyirongo.
Nditafika ndidaima pawindo ndipo ndidamva awiriwo akulankhula. Apa ndidadzutsa eni nyumbazo kuti andikhalire umboni. Ndipo titagogoda, Nyirongo adatitsekulira koma adakanitsitsa zoti mkazi wanga adali mnyumbamo, Luhanga adalongosola motero.
Bamboyo adati adamulonjeza Nyirongo kuti ampatsa K10 000 ngati mkazi wakeyo sadali mnyumbamo.
Adanditsekulira ndipo nditangoti lowu, adandiponyera chikwanje pamutu chomwe chidandiphonya ndi kumenya feremu ya chitseko, kenaka adandimenya ndi chitsulo padiso ndi pamutu ndipo ndidagwa pansi. Apa nkuti mkazi wanga atathawira pawindo, bamboyo adatero.
Iye adati atadzuka adakuwa kuti: Wakuba! Wakuba! ndipo anthu ozungulira adamugwira mkaziyo nkuyamba kummenya.
Iye adati adaleretsa mkazi wakeyo mmanja mwa anthu okwiyawo ali buno bwamuswe ndipo adamupititsa kupolisi achisoni atamuponyera kachitenje. Luhanga adati adatengera mkazi wake kupolisiko pomuganizira kuti waba ndalama kaamba koti ndalama yomwe adali atatolerayo adali atamupatsa Nyirongo poti awiriwo amakonzekera zothawira ku Lilongwe.
Ndidatengana ndi apolisi kuti tidzamutenge Nyirongo, koma sitidamupeze. Ndidadzidzimuka kumva kuti wapezeka atadzimangirira, adatero Luhanga.
Pakadalipano mkaziyu akubindikira mnyumba kaamba ka manyazi ndi zomwe zidachitikazi chifukwa akatuluka anthu amangomulozaloza. Adakana kutuluka kuchipinda pomwe Msangulutso udafuna kumva mbali yake.
Mkucheza kwathu ndi mayi a wodzikhwezayo, mayi Nyamhone, iwo adati adazindikira kuti mwana wawoyo adadzimangilira nthawi ili mma 4 kololo mmawa wa Lachitatu ndipo sadasiye uthenga uliwonse.
A Nyamhone, omwe amagulitsa masuku, adati anzake ndi amene adawauza kuti mtengo womwe uli pafupi ndi nyumba yawo mukulendewera munthu.
Mayiwo adati mwana wawoyo, yemwe wasiya ana awiri ndipo banja lake lidatha mchaka cha 2010, adadzamugogodera cha pakati pa usiku ati kukangowaona.
Nyamhone adati Nyirongo adadzimangirira mumtengo wautali kwambiri ndipo pa nthawi yomwe adamuonayo adali asanamalizike koma kuti anthu sadakwanitse kukwera kuti amuombole.
Mwana wanga sadayambane ndi munthu aliyense ndipo sadandilongosolere kalikonse zokhudza mzimayi, a Nyamhone adatero.
Iwo adati koma adali okhumudwa ndi apolisi omwe ngakhale adauzidwa za ngoziyo mmawa adafika pamalopo 12 koloko masana ndipo thupilo sadalitengerenso kuchipatala ati kaamba koti lidali litayamba kale kufufuma.
| 15 |
Mabungwe athotha galu wakuda ku MJ Anthu mboma la Mulanje omwe adakhudzidwa ndi njala kaamba ka ngozi za kusefukira kwa madzi komanso chilala kumayambiriro a chaka chino akuombera kuphazi mabungwe angapo atamva pempho lawo la kufunika kwa chakudya kuti apulumutse miyoyo yawo ku njala.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mabungwe a Oxfam, Save the Children, Goal Malawi, Concern Universal, Irish Aid ndi ena ndiwo adachita chamuna posonkha ndalama zoposa K7 biliyoni zomwe zathandiza kuti galu wakuda yemwe adadutsa mbomali ayambe kuona msana wa njira.
Gogo kutsekulitsa akaunthi ya Airtel Money Mwambo wokhazikitsa chithandizochi udachitika ku Mulanje sabata yatha pamene akuluakulu a mabungwewa komanso mafumu adachitira umboni kuyamba kwa ntchito yothandiza anthu ovutika ndi njalawa.
Kazembe wa dziko la Norway ku Malawi, Kikkan Haugen, adati pofuna kuonetsetsa kuti palibe chinyengo pa ndondomeko yothandiza anthuwa, mgwirizano wawo wasankha kampani ya foni zammanja ya Airtel kuti anthu azilandira chithandizo cha ndalama zogulira chimanga, mafuta ophikira ndi nyemba kapena nandolo kudzera ku kampaniyi.
Wogwirizira udindo wa mkulu wa kampani ya Airtel, Charles Kamoto, adati kampani yawo ithandizira ndondomekoyi kudzera mu Airtel Money.
Chomwe chizichitika nchakuti mwezi uliwonse munthu aliyense [amene ali pamndandanda wolandira nawo thandizoli] azilandira K15 800 yoti agulire thumba limodzi la chimanga, malita awiri a mafuta ophikira ndi nyemba kapena nandolo zolemera makilogalamu 10.
Ndiye chomwe tapanga nchoti aliyense tamutsekulira akaunti ya Airtel Money yomwe azilandirirako ndalamayo. Ndipo zikalowa atha kupita kwa maejenti anthu amene ali mboma lomwelino kukatenga ndalamazo zokagulira chakudya, adatero Kamoto.
Malinga ndi Haugen, ndalamazi zizitumizidwa mwezi uliwonse kuti anthu asatuwe ndi njala.
| 4 |
Mavuto a ambulasi anyanya mzipatala Ndi Lachiwiri mmawa. Tili pafupi ndi nyumba yachisoni pachipatala cha Gulupu mu mzinda wa Blantyre. Rose Kaphesi, mwana wake ndi achibale atambalala padzuwa. Maso ali kunjira kudikira ambulasi.
Sabata yatha chitulukireni mchipatala, koma ambulasi yoti iwatengere kumudzi kwawo ku Nsanje palibe.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Sindikudziwa kuti ambulasi ibwera liti. Timayenera tinyamuke Lamulungu koma mpaka lero, adatero Kaphesi.
Awa ndiye mavuto omwe ayanga mzipatala za boma mdziko muno zomwe zakhumudwitsa mkulu wa bungwe lopititsa patsogolo ntchito zaumoyo la Malawi Health Equity Network (Mhen), George Jobe.
Tamvani yapezanso kuti amayi 15 adaberekera panjira chaka chino chokha pachipatala chachingono cha Kandeu mboma la Ntcheu pamene amapita kuchipatala cha boma cha Ntcheu kuti akathandizidwe.
Mmodzi mwa ogwira ntchito pachipatalapo, amene sadafune kutchulidwa, adati vuto lakusowa kwa ambulasi lafika powawa.
Tidauzidwa kuti tilandira ambulasi mu 2009, adati timange malo wosungira ambulasiyo koma mpaka pano kuli chuu! iye adatero.
Kandeu ili pamtunda wa makilomita 36 kukafika kuchipatala chaboma. Anthu akuti amatengedwa pa machila kapena panjinga popita kuchipatala chachikulu.
Nthawi zina amatengedwa pa matola ndipo amalipira K20 000 kuti akawasiye kuchipatala, adaonjeza wachipatalayu. Chaka chino chokha anthu 15 aberekera panjira ndipo mmodzi adamwalira mnjira.
Nako kuchipatala cha Chilipa mboma la Mangochi akuti anthu awiri amwalira chaka chino pamene amadikirira ambulasi kuti idzawatenge.
Wapampando wa chipatala cha Chilipa, nyakwawa Nkaya ya mdera la T/A Chilipa, yati ali ndi ambulasi imodzi yokha yomwe ikutumikira zipatala zisanu.
Tili ndi chipatala cha Chilipa, Katema, Mtimabi, Phirilongwe ndi Kapire komwe ikutumikira. Ndi mitunda yotalikirana ndi makilomita 40 komanso misewu yake siyabwino, idatero mfumuyi.
Iye wati wakhala akudandaula koma yankho palibe. Kuti ambulasi ichokere ku Mtimabi kudzafika ku Chilipa, ndi nthawi yaitali. Izi ndizomwe zidachititsa kuti anthu awiri amwalire amene amafunika atumizidwe kuchipatala cha Mangochi, adatero Nkaya.
Pachipatala cha Masasa ku Dedza ndi Balaka odwala amawauza kuti agule mafuta kuti ambulasi iwatumikire.
Pachipatala chaboma cha Rumphi, mavuto akulanso malinga ndi mneneri wachipatalachi Bwanalori Mwamlima.
Tidali ndi ambulasi 6, pano 4 sizikuyenda. Mavuto alipo kuti tikafike ku Hewe komwe ndi mtunda wa makilomota 60, adatero Mwamlima.
Chipatala cha Nkhotakota pali ambulasi imodzi yokha. Mkulu pachipatalachi Jimmy Phiri wati kusayenda kwa ambulasi zina kwadzetsa mavuto akulu.
Koma Jobe akuganiza kuti unduna wa zaumoyo udakapatsidwa ndalama zambiri mavutowa akadachepa.
Tili ndi mavuto ambiri mzipatala amene akufunika ndalama zambiri. Pali mavuto azakudya komanso mayendedwe. Mavutowa kuti athe pakufunika ndalama zambiri.
Maboma ena ali ndi ambulasi koma akulephera kukonzetsa. Ena vuto ndi kuchepa kwa madalaivala. Nthawi zina vuto ndi mafuta womwe akuchititsa kuti wodwala azisonkha ndalama kuti ambulasi iyende. Izi nzachisoni ndipo boma lichitepo kanthu msanga, adaonjeza Jobe.
Mmodzi mwa akuluakulu aku unduna wa zaumoyo Beston Chisamile wati boma lili ndi mapulani ogula ambulasi zina.
Mavuto alipo koma tili ndi mapulani oti tigule ambulasi zina, adatero Chisamile.
| 6 |
Subsets and Splits