Text
stringlengths 292
6.6k
| labels
int64 0
19
|
---|---|
Mmalawi Mulibe Ebola-Unduna Kafukufuku yemwe akatswiri a za chipatala mdziko la South Africa achita, watsikimiza kuti munthu wa mboma la Karonga amene wamwalira atadwala matenda ofanana ndi Ebola samadwala matendawa.
Chikalata chomwe unduna wa zaumoyo watulutsa lachiwiri, chatsikimizira a Malawi kuti asakhale ndi nkhawa chifukwa padakali pano, mdziko muno mulibe nthenda-yi.
Masiku apitawa nkhawa inakula mdziko muno pamene mkulu wina wa mboma la Karonga anamugoneka pa chipatala chachikulu cha bomalo yemwe anali ndi zizindikiro zina za nthendayi.
Mkuluyu wamwalira lachiwiri lapitali ndipo wayikidwa mmanda usiku wa tsiku lomweli ndi a zachipatala okhaokha omwe anavala zozitetezera zomwe ena anayamba kuganiza kuti mkuluyu wafa ndi ebola.
Padakalipano unduna wa zaumoyo wapempha a Malawi kuti akhale mtima pansi kaamba koti kafukufuku yemwe bungwe la National Institute of Communicable Diseases lachita, wasonyeza kuti nthenda yomwe amadwala mkuluyu si Ebola.
Chikalatachi chomwe wasayina ndi mlembi wamkulu mu unduna wa zaumoyo Dr. Dan Namalika chati nkhani za zaumoyo zimayendetsa mwachinsinsi kaamba koti zimakhudza ufulu wa anthu.
Iwo ati apitilira kukhwimitsa chitetezo komanso kuteteza anthu ku nthendayi.
| 6 |
Kusanthula khansa ya mmawere Petani Mtonga, wachiwiri kwa mkulu wa nthambi ya matenda a khansa kuchipatala cha Queen Elizabeth mumzinda wa Blantyre wati matenda akhansa akagwira mawere amatchedwa khansa ya mmawere.
Sabata yatha, Mtonga adati matenda a khansa alipo a mitundu ingapo.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Malinga ndi dotoloyu, khansa ya mmawere imagwira amayi omwe afika msinkhu wobereka ndipo imatha kufalikira kuziwalo zina ngati matendawa azindikiridwa mochedwa.
Amayi ayenera kudziyesa kaye okha matendawa Sabata yatha ndidafotokoza bwino lomwe kuti kwambiri matenda a khansa amayamba okha kotero sizitengera kuti ndi chiwalo chanji chomwe chakhudzidwa ndi matendawa choncho mai aliyense amakhala pachiopsezo cha khansa ya mmawere. Ngakhale izi zili chomwechi, amayi osuta fodya komanso oledzera amakhala pachiopsezo chachikulu chifukwa mufodya ndi mowa mmapezeka zinthu zomwe zimakolezera matendawa, iye adatero.
Dotoloyu adati zizindikiro za khansa ya mmawere ndi monga kutuluka zotupa mmawere, kuchita zilonda mmawere, kutulutsa magazi mmawere ndi kusintha mtundu kwa mawere.
Iye adati mayi wina aliyense, makamaka yemwe wafika msinkhu wobereka amayenera kumadziyeza yekha pamene akusamba kapena akamaliza kuti ngati angaone zinthu zodabwitsa, athamangire kuchipatala ndipo pakutero, imazindikiridwa mwachangu.
Amayenera kumadziyanganira pagalasi makamaka lalikulu lapakhoma kuti athe kumadziona bwinobwino ataimirira ndipo akaona kuti bere kapena mawere asintha mtundu kapena akuoneka kukula kusiyana ndi poyamba, athamangire kuchipatala.
Njira ina, mayi amatha kuimirira kapena kugona pansi ndi kuyamba kusindikiza bere lakumanzere ndi chikhatho chamkono wakumanja mozungulira, ndi kubwerezanso ndi bere lakumanja momvetserera bwino ndipo akaona kuti mukumveka kanthu kalikonse kachilendo, athamangire ku chipatala, iye adatero.
| 6 |
Koma pa Wenela zidzatheka? Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Tsikulo tidakhala pa Wenela. Tidali kusowa cholankhula. Kodi ndi January ameneyu? Ayi ndithu. Kukazinga chimanga chisanachoke mmunda.
Nyimbo zomwe ankaika Gervazzio tsikulo palibe icho ndinkatolapo. Mvula idali ikugwa.
Wamkana ku Europe! Wamkana ku America! Wamkana mwana wake! Iyinso nyimbo idali kuphulika pomwe tidamva kuti ndege zidali kutera pa Wenela. Pajatu pa Wenela pali bwalo la ndege.
Tidangomva mkokomo wa ndege.
Timayesa ikutera.
Inkatera.
Koma siyidali ndege.
Lidali lichero.
Tonse tidathawa! Licherolo mudali Joloji Chadyaka yemwe ena amayembekezera kuti afikira ku Lumbadzi. Koma abale anzanga, ngati kuli munthu amene ndimadabwa naye, ndiye ndi ameneyu.
Nanga inu, munthu anganene za kutsitsa mpweya nkumatsika lichero pa Wenela mungadabwe nazo? Komatu nkokomo umene unkamveka pa Wenela aliyense adathawa.
Tsono. Tsono. Tsono.
Sindinadabwe ndi za Chadyaka. Chadyaka ndi Chadyaka basi kaya munena za mmera, kaya soya, kaya nsetanyani, kaya thonje. Chadyaka ndi chadyaka basi! Ndimamukumbuka mkulu ameneyu.
Adayenera kufika ku ukwati wa mwana wa mnzanga 2 koloko. Mwambowo umayenera kutha 4 koloko. Iye adafika 4:20pm.
Inetu zonena zambiri ndilibe.
Ndiye mwati anthu otchuka atatu anabwera pa Wenela nthawi imodzi? Mwati uyu Dona adatenga Melise ndi Davide anafika pa dambwe lathu ku Kumbali wafika mdziko muno kudzatenga ana ena? Bwanji osatenga nkhalamba ya chibwana Joloji Chadyaka? Bwanji osatenga Moya Pete? Ndiye mwati kwafikanso uyu Rihhhhon? Pakadakhala kuti Abiti Patuma alipo nkadamufunsa, koma anali atapita kofufuza nkhanizo. Pa Wenela panalibepo.
| 15 |
Kaundula wa mavoti akuyenda bwino Anthu kulembetsa msabatayi A Malawi mmadera ena adakhamukira kumalo olembetsa maina awo mkaundula wa chisankho cha pa 20 May 2014.
Malinga ndi mphunzitsi wa za ndale kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, izi ndi chisonyezo chakuti anthu ali ndi njala yofuna kusankha atsogoleri awo, zimene zingachititse boma la PP kugwa, kapena kulamuliranso zaka zina zisanu.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Chinsinga amalankhula izi malinga ndi momwe ntchito ya gawo loyamba la kalembera wa chisankho mmaboma a Chikhwawa, Nsanje, Neno, Mwanza ndi madera ena mboma la Blantyre yayambira.
Kalemberayu adayamba Lolemba pa 22 July ndipo mmaderawa atseka pa 4 August 2013.
Malinga ndi Elton Kananji yemwe akuyanganira kalemberayu pamalo wolembetsera pa sukulu ya pulaiveti ya Che Mussa Assemblies of God mumzinda wa Blantyre adati anthu akulembetsa mwa unyinji.
Iye adati Lolemba anthu 342 ndiwo adalembetsa. Mwa anthuwa, 172 ndi amuna pomwe 170 adali amayi.
Apa ndiye zili bwino pokhala tsiku loyamba kulembetsa. Lero [Lachiwiri] anthu akubwerabe mwa unyinji zomwe zikusonyeza kuti anthu ayirandira ntchitoyi mokhulupirika, adatero Kananji.
Nako ku Mwanza anthu akuti adapita kukalembetsa mwa unyinji. Monga akufotokozera T/A Nthache ya mbomalo, anthu akufuna kudzavota kuti adzasinthe boma kapena kulibwezeretsa.
Ndinakalembetsa atangotsekula, kuno tikulembetsera pasukulu ya pulaimale ya Lipongwe. Anthu akukhamuka mwa unyinji zomwe zikusonyeza kuti aliyense ali ndi chidwi chofuna kudzavota, adatero Nthache.
Nako ku Neno anthu akuti ali kalikiliki kukalembetsa kalemberayu. Malinga ndi Francis Pulula wa kwa Senior Chief Saimoni mbomalo, akufunitsitsa atadzavota mu 2014.
Iye adati chisankho chobweretsa boma lina kapena kuti boma lilipoli lipitirize chili mmanja mwake zomwe waona kuti ndi bwino akalembetse.
Tikulembetsera pasukulu ya pulaimale ya Lisungwi. Anthu akulembetsa mwa unyinji moti nane vuto nkuti ndinatangwanika ndi ntchito koma nthawi iliyonse ndikukalembetsa, adatero.
Ku Nsanje zonse akuti zinali tayale kuyambira Lolemba mpaka Lachiwiri pomwe timacheza ndi Senior Chief Malemia ya mbomalo.
Anthu akuti amalembetsa mwa unyinji ngakhale panali vuto limodzi kumeneko.
Pamzere tikukhala nthawi yaitali kuti tithandizidwe zomwe si zabwino. Akumachedwa kuti atithandize ndiye ena zikumawagwetsa mphwayi kuti akaime pamzere nthawi yaitali, adatero Malemia.
Chinsinga adati chisankhochi ndi chofunika kwambiri. Simungadabwe kuona anthu akukhala padzuwa kuti alembetse. Anthu adziwe kuti zonse ndi zotheka ngati atakalembetsa kuti adzakhale ndi mwayi wodzavota, adatero Chinsinga.
Mneneri wa bungwe loyendetsa chisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) Sangwani Mwafulirwa wati kalemberayu wayamba mwa mkokomo ndipo pofika Lachiwiri padalibe mavuto omwe adawoneka.
Mwafulirwa adati ngati padali vuto lomwe amaliganiza kuti lingasokoneze ndi la ngozi yomwe idachitika ku Chikhwawa komwe galimoto yomwe idatenga ogwira ntchito a bungwe la MEC omwe amafuna akaphunzitse za ubwino ubwino wokalembetsa idachita ngozi Lolemba.
Galimotoyo idazima ndiye pomwe amati ayilizenso mabuleki sadagwire ndiye idayamba kubwerera mmbuyo. Dalaivala adayesetsa kuti asabwerere mmbuyo koma zidalephereka mpaka kukatsamira nyumba ina. Ogwira ntchito ku MEC adavulala ndipo adawatengera kuchipatala komwe adawathandiza, adatero mneneriyu.
Pa za momwe anthu ayambira kulembetsa, Mwafulirwa adati akukhulupirira kuti ntchitoyi itha bwino komanso kuti zawapatsa chikhulupiriro kuti maphunziro omwe adachititsa kuti anthu akalembetse agwira ntchito.
Kumbali ya mavuto omwe Senior Chief Malemia yadandaula ku Nsanje, Mwafulirwa adati afufuza ngati pali vuto loti alowererepo kapena ngati vuto ndi kuchepa kwa olembetsa kalemberawo.
Dziko lino pa May 20, 2014 lidzachititsa chisankho chapatatu. Anthu adzasankha khansala wa wodi yawo, phungu wa Nyumba ya Malamulo ndi mtsogoleri wa dziko.
Anthu omwe alembetse ndiwo adzakhale ndi mwayi wodzasankha mtsogoleri wawo. Malo olembetserawo akumatsekulidwa 8 koloko mmawa ndi kutsekedwa 4 koloko madzulo.
Malowa akumatsekulidwa tsiku lililonse.
Ndipo MacArthur Matukuta, yemwe ndi mkulu wa gulu la zisudzo la Solomonic Peacocks, wati ntchito yophunzitsa anthu ubwino wokalembetsa ndi kudzavota ikuyenda bwino.
Takhala tikugwira ntchito yotere pa zisankho za 1999 ndi 2004 koma kunena zoona chaka chino zikuyenda. Tikufalitsa uthenga wachisankho kupyolera mzisudzo ndipo anthu akuulandira, adatero Matukuta gulu lake likuchita zisudzozo mumzinda wa Blantyre..
| 11 |
CWO Ipempha Amayi Atenge Gawo pa Mlozo Bungwe la amayi achikatolika la Catholic Women Organisation (CWO) mu arkdayosizi ya Blantyre lapempha amayi onse a mpingowu kutengapo mbali pa mlozo wa zochitikachitika womwe bungweli lakonza mchaka chino cha 2020.
Ena mwa amayi achikatolika mu Blantyre archdiocese Mlembi wa bungweli mu arkdayosiziyi mayi Hellen Maseko ndiwo alankhula izi ku Limbe Cathedral mu arkdayosiziyi pambuyo pamkumano wa atsogoleri a bungweli womwe cholinga chake ndikukonza mlozo wa zochitika (Action Plan) zomwe bungweli lichite mchaka chino chatsopano.
Mayi Maseko ati mlozo watsopanowu uli ndi zochitika zosiyanasiyana mogwirizana ndi ma pulojekiti omwe bungweli lili nawo zomwe anati ngati amayiwa agwirana manja zithandiza kukweza miyoyo yawo pa uzimu komanso chitukuko cha iwo eni cha ku thupi.
Ndi zoona takumanadi ndi cholinga choti tikonze mlozo wa momwe tiyendere mchakachi. Mlozowu tayikamo zinthu zambiri potengera ndi ma pulojekiti omwe tili nawo ngati amayi. Mchaka cha 2019 zonse zimene zinali mu action plan yathu tinakwaniritsa ndipo palibe chomwe tinalephera kamba koti amayi onse anatenga mbali choncho chaka chino tilinso ndi chikhulupiliro kuti amayi onse opezeka mmaparish 43 mu arkdayosiziyi atithandizanso. anatero mayi Maseko.
Iwo atinso ngati amayi akufunitsitsa kuti achite zotheka kuti azikhala odzidalira pa moyo wao wa tsiku ndi tsiku kwinakunso akutumikira mpingo wao.
Nthawi yoti ngati amayi kukumana kungochita mapemphero mkumapita inatha. Nthawi ino ndiyoti tilumikize moyo wa mapemphero ndiponso kuzidalira kwa amayi pa moyo watsiku ndi tsiku. Ndiye tikagwirana manja ndiye kuti dayosizi yathu ikhala yotsogola, komanso amayi athu akhala otukuka mu uzimu ndi ku thupi komwe.
Mu Mlozowu ati chochitika choyambilira cha amayiwa ndi kukhazikitsa ntchito yobzala mitengo yomwe amayiwa amathandizidwa ndi banki la National ku parishi ya Kadikira pa 25 January, 2020 komwenso kukumbekezereka kukhala arkepiskopi wa arkdayosiziyi Ambuye Thomas Luke Msusa komanso akuluakulu ochokera ku banki ya National.
| 13 |
Agumula nyumba pokaikira masalamusi Mbuto ya kalulu idakula ntadzaonani. Mwambiwu udapherezera Lachiwiri ku Lilongwe pomwe anthu okwiya ku Mtsiriza adagumula nyumba ya banja lina ati powaganizira kuti amazembetsa anthu mmatsenga.
Anthuwo sadalekere pomwepo, koma kuotcha galimoto lapolisi lomwe apolisi adakwera kuti akateteze banja la Malunga amene adaotcheredwa nyumbayo.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mneneri wa likulu la apolisi James Kadadzera watsimikiza za chipolowecho ndipo wati apolisi agwira anthu 20 omwe akuwaganizira kuti akukhudzidwa pa chipolowecho.
Kadadzera: Tilibe lipoti Awa tawagwira ngati poyambira kafukufuku ofuna kupeza chenicheni chomwe chidachitika chifukwa pakumveka nkhani zosiyanasiyana ngakhale mphekesera yaikulu ikukhudza za masilamusi, adatero iye.
Polankhula ndi Msangulutso, anthu omwe adaona izi zikuchitika adati banjalo amalikaikira kuti limasowetsa anthu mmatsenga ndipo patsikulo, munthu wina yemwe amalira momvetsa chisoni adawauza kuti Mulungu adamuonetsa vumbulutso akupephera kuti mbale wake yemwe adasowa akusungidwa mnyumbamo.
Mmodzi mwa anthuwo, Enifa Kaira, adati mphekeserayo itamveka anthu adayamba kusonkhana panyumbapo uku akukalipa kuti eni nyumbayo atulutse anthu onse omwe amawasunga mmatsenga.
Kudali khamu la anthu: Ana, akulu ndi okalamba kufuna kuonetsetsa kuti mnyumbamo mutuluka chiyani. Eni nyumbayo ataona kuti zinthu zikuonjeza, adamuuza odandaulayo kuti alowe mnyumbamo akayangane mbale wakeyo koma naye sadatuluke mpaka apolisi adafika, adatero iye.
Kaira adati apolisi atafika adathamangira mnyumbamo ndipo potuluka adatenga odandaulayo ndi eni nyumbayo nkuwakweza galimoto ya polisi kuti azipita nawo koma anthu sadakondwe nazo ndipo adayamba kugenda apolisiwo nkuwayatsira galimotoyo.
Mwana wamkulu wa mnyumbamo Mwayi Malunga, wa zaka 24, yemwe adali pakhomo pomwe izi zimachitika adati zomwe anthuwo adachita lidali dumbo chabe poti anthu mderalo safunira banjalo zabwino.
Iye adati pomwe zonse zidayamba mma 3 koloko masana iye akupuma ndipo amamvera phokoso la anthu kutulo osadziwa kuti kukuchitika chiyani mpaka pomwe mayi ake adamudzutsa kuti akaone zomwe zikuchitika kunja.
Malunga adati atatuluka panja adaona khamu la anthu likusokosa uku likuloza nyumbayo pakati pawo pali munthu wa mtsikana akulira uku akuti akufuna mbale wake yemwe ali mnyumbamo.
Pokana milandu, tidamupatsa mwayi woti alowe mnyumbamo ayangane paliponse ndipo adafufuzadi koma osapeza kanthu kenako tidangoona wagwa nkukhala ngati wakomoka mpaka pomwe apolisi amafika, adatero Malunga.
Iye adati apolisiwo akuti azinyamuka ndi munthuyo komanso makolo ake, anthu adayamba kuwakuwiza kenako kugenda koma apolisiwo adaliza galimoto yawo ndipo asadafike patali, anthuwo adayiyatsa iwo nkuthawa.
Mnyamatayo adati anthuwo adayamba kugenda nyumba yawo mpaka kuswa magalasi onse, chitseko komanso ena adakanganula malata mbali imodzi nkugwetsa mpanda wa njerwa komanso kuzula chitseko cha mpandawo nkunyamula.
Zidali zachidziwikire kuti kwinako zidalowa kuba basi osati zomwe amanenazo chifukwa mpaka pano munthu yemwe amati tikusungayo sadamupeze, adatero iye.
Kadadzera adati chodabwitsa nchakuti apolisi alibe lipoti lokhudza munthu yemwe akuti adasowayo komanso atachita chipikisheni mnyumbamo sadapezemo munthu wosonyeza kuti amasungidwa mobedwa.
| 19 |
Vatican Ilandira Anthu 33 Othawa Kwawo A kulikulu la mpingo wa katolika ku Vatican lachinayi akuyembekezeka kulandira anthu othawa kwao okwana 33 omwe akuchokera ku chilumba cha Lesbos mdziko la Greece ndipo anthu ena khumi akuyembekezeka kufikanso mwezi omwe uno.
Malipoti a Catholic News Agency ati anthuwa ndi ochokera mmaiko a Afghanistan, Togo komanso Cameroon.
Izi zadza potsatira pempho la mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco lakuti a ku likulu la mpingowu akuyenera kupereka thandizo kwa achinyamata komanso mabanja omwe amathawa mmaiko awo kaamba ka kusamvana mmaikowo zomwe zimadzetsa nkhondo.
Anthuwa akhala akuthandizidwa ndi ofesi ya a Papa yoona zachifundo, bungwe la Saint Egidio komanso gulu la akatolika omwe amathandiza anthu osauka.
| 14 |
Radio Maria Malawi Yatsegulira Mariatona Mwambo otsekulira Mariatona ku Radio Maria Malawi, wachitika lero ku likulu la wailesiyi mboma la Mangochi.
Mwambowu watsekulidwa, utayimitsidwa kaye masiku apitawa chifukwa cha kubuka kwa mliri wa Covid-19.
Miyambo ngati iyi siyichitika pa Mariatonayu A Director a wailesiyi, bambo Joseph Kimu, ati wailesiyi yachita izi kaamba koti imadalira thandizo la anthu kuti igwire ntchito zake, pamene mwa zina, imagwiritsa ntchito mwambo wa Mariatona, pomwe omvera amawonjezera kudzipereka kwawo popereka thandizo lawo, kuti ntchito zawailesiyi zidzipita patsogolo.
Monga mwachizolowezi chaka ndi chaka timachita Mariatona kupempha chithandizo kwa anthu popeza malamulo amatiletsa kuchita malonda ambiri pa wailesi mmalo mwake njira iyiyi ndi yomwe timapezera chithandizo, anatero bambo Kimu.
Iwo apempha akhritsu akufuna kwabwino kuti atenge mbali pothandiza wailesiyi popeza Mariatnayu asiyana ndi wa zaka za mbuyomu ndipo adalira kwambiri ma pologalamu a pawailesi osati kuyenda mma parish.
| 13 |
COVID-19 Ilipodi-Action Hope Bungwe la Action Hope Malawi ladzudzula mchitidwe omwe anthu ena akulimbikitsa popereka mauthenga a bodza ku mtundu wa a Malawi kuti kulibe kachirombo ka Coronavirus.
Aaron: Tikanena kuti kulibe, tikulakwitsa Mkulu wa bungweli mdziko muno a Sammy Aaron anena izi pomwe Radio Maria Malawi imafuna kumva za kuopsa kwa mchitidwewu.
Iwo ati mchitidwewu utha kupangitsa kuti anthu ambiri akhudzidwe ndi mliriwu.
Tikanena kuti matenda amenewa kulibe tikulakwitsa kwambiri kamba koti matendawa akuwonoga miyoyo yambiri mdziko lapansi pano, anatero a Aaron.
Iwo apempha a Malawi kuti apitirize kupewa matendawa pochita zomwe unduna wa zaumoyo ukupempha.
Pofika tsiku la lero anthu oposa 500 ndi omwe apezeka ndi kachirombo ka Corona virus ndipo asanu ndi omwe amwalira.
| 6 |
Singanga Akagwira Ukayidi Zaka 11 Kamba Kogwililira Bwalo la milandu mboma la Chikwawa, lachitatu lalamula singanga wina kuti akakhale ku ndende kwa zaka 11 atapezeka olakwa pa mlandu ogwililira msungwana wa zaka 13.
Singanga kuchita zomwe amadziwa bwino pa ntchito yake Bwaloli linamva kuchokera kwa woyimira boma pa mlandu Sergeant Emmanuel Namarwa Kuti a Lawrence Chandendema anapempha singangayu yemwe dzina lake ndi Goodson Bandecha, kuti apereke chithandizo kwa ana ake aakazi atatu omwe amavutika ndi kupweteka kwa mmimba. Bandecha akuti anavomera kugwira ntchitoyi koma anati azichitira izi mkachipinda kena komwe anawa amalowa mmodzi mmodzi.
Mchipindamu mutalowa msungwana wa zaka 13 singangayu anamulamula kuti avule zovala zonse ndi kugona pa mphasa yomwe inali mkachipindako ndipo pambuyo pake anamugwililira. Atakawonekera ku bwaloli, Bandecha anaukana mlanduwu zomwe zinachititsa a mbali ya boma kuti abweretse mboni zisanu zomwe zichititsa kuti mkuluyu apezeke olakwa.
Ndipo popereka chigamulo chake First Grade Magistrate Gladstone Chilundu anati wapereka chilango cha mtunduwu kuti ena atengerepo phunziro kaamba koti milandu ya mtunduwu ikuchulukira mbomalo komanso ponena kuti singangayu anachita kukonzekera kuti achite izi.
Goodson Bandecha yemwe ndi wa zaka 44, amachokera mmudzi mwa Wizalamu kwa mfumu yaikulu Mphuka mboma la Thyolo.
| 7 |
Kwelepeta Wayamikira Mabungwe Pothandiza Asilamu ndi Chakudya Mnyengo ya Ramadhan Phungu wa dera la Zomba Malosa, Grace Kwelepeta wayamikira mabungwe a Malawi Relief Fund UK komanso Issa Foundation kaamba kothandidza anthu a mdera lake omwe ndi a chipembezo cha chisilamu, ndi katundu wosiyanasiyana wa chakudya pomwe akukonzekera nyengo ya Ramadhan.
Kwelepeta yemwenso ndi wachiwiri kwa nduna yowona za kusasiyana pakati pa amayi ndi abambo wayankhula izi lachinayi ku Zomba pomwe anali mlendo wolemekezeka pa mwambo wopereka chakudya chochokera ku mabungwe awiriwa.
Iye wati chifukwa cha kubwera kwa muliri wa Coronavirus, aganiza kuti chaka chino asagawe chakudya kudzera mmizikiti koma awapatse zinthu zoti azikaphika ndi kudya kunyumba kwawo kuwopa kupatsirana kachilomboka.
Nyengo ya Ramadhan ya chaka chino ndi yosiyana ndi ya zaka zinazi chifukwa anthuwa samadyeraso limodzi ngati kale koma mmalo mwake tangowagawira kuti aliyense azikadyera kwawo, anatero Kwelepeta.
Poyankhulapo mmodzi mwa akuluakulu ku bungwe la Malawi Relief Fund UK, mayi Doreen Kawanda ati chakudyachi chiwathandidza anthuwa pa nyengo ya Ramadhan komanso nyengo ino ya mliri wa Coronavirus. Mayi Kawanda akufotokoza.
Monga momwe tikudziwira kuti maiko ambiri kuphatikiza kuno ku Malawi kwakhudzidwa ndi matendawa tinayesetsa kupeza njira yoti anthuwa alandire chakudya chimenechi posatira zomwe a WHO akulimbikisa, anatero a Kawanda.
| 13 |
Makhansala ayamba mopendama Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Ngakhale kuli makhansala, ena akadatunga madzi kutali Pamene pangodutsa miyezi 4 chisankhireni makhansala, anthu ena akudandaula kuti makhansalawa ayamba kubisala ndipo sakuwayendera kuti amve mavuto awo.
Mwachitsanzo, kwa gulupu Soka, T/A Dambe mboma la Neno akuti khansala wawo adamuona nthawi ya kampeni yokha ndipo chimusankhire sakufikanso.
Kuderali kuli mavuto monga kusowa madzi aukhondo, midzi 34 kumeneku ikumwa mjigo umodzi komanso kuli mavuto a kusowa zipatala pomwe anthu akuyenda makilomita 26 kuti akafike kuchipatala cha boma cha Neno.
Koma khansala wa derali Montfort Bwanali adati nzoonadi kuti sadafikeko kuderalo komanso madera ena kaamba ka mavuto a mayendedwe.
Kupatula K80 000 yomwe khansalayu akulandira pamwezi, boma lidati makhansalawa apatsidwanso mwayi wotenga njinga yamoto mwa ngongole kuti ziwathandize kuyendera madera awo. Mpaka lero lonjezoli silidakwaniritsidwe zomwe zikubweretsa mavuto amayendedwe monga Bwanali adafotokozera.
Kunyamuka cha mma 4 mmawa kuti ukafike midzi imeneyi yomwe yachita malire ndi dziko la Mozambique ndi mma 2:00 madzulo. Apatu ndiye kuti wayenda pagalimoto ndiye nzovuta kuti ndingawayendere wamba anthu amenewa pokhapokha nditakhala ndi mayendedwe, adatero Bwanali amene wati chisankhidwireni wangogwira ntchito kamodzi.
Iye adati ntchitoyo idali yolambula msewu sabata yatha.
Izi tsopano zikuchititsa kuti anthu asaone ubwino wa makhansala monga midzi ya Kumphika, Kuziona, Ntaja, Soka, Benalita, Leketa, kwa Kunenekude ndi ina ku Mwanza ndi Neno pamene akusowabe kotulira nkhawa zawo.
Nyakwawa Kuziona yati anthu ake akuona mavuto ambiri amene amafunitsitsa atawatula kwa khansala wawo amene sakuoneka.
Mwaona nokha kuti midzi yonse kuno tikumwa mjigo umodzi, tilibe mijigo. Tilibe sukulu ya sekondale, tikafuna kuchipatala ndiye kuti tiyende makilomita 26 kukafika kuboma la Neno. Mwaonanso kuti timalima kwambiri koma sitingathe kupita nazo kumsika kaamba ka kusowa kwa misewu.
Nthawi yomwe adati tikhala ndi makhansala ndidasangalala poganizira kuti tizidzalankhulana ndi khansala wathu kumuuza mavuto athuwa. Koma chisankhireni khansala mpaka lero sadafike kuno, idatero mfumuyo.
Vutoli liliponso mmudzi mwa Thambala kwa T/A Kanduku mboma la Mwanza. Midzi inaso mboma la Ntcheu kwa T/A Phambala ikudandaula kuti khansala wawo adasowa atangomusankha.
Koma izi zikusiyanabe ndi mmudzi mwa Mtamba kwa T/A Nkalo mboma la Chiradzulu komanso mmudzi mwa Chimpini mboma la Zomba. Kumeneko ntchito za khansala akuti zayamba kuoneka ngakhale kukuvutabe kuti alumikizane ndi khansala wawo.
Mfumu Mtamba ikuti kumeneko khansala wawo akumawayendera ndipo wawabweretsera khitchini lophikira phala la ana asukulu.
Nayo nyakwawa Golosi ikuti chiyembekezo chikuoneka kuti makhansalawa awathandiza kudera lawo ngakhale akusowa nthawi yomamva mavuto amene akukumana ndi anthu awo.
Khansala wa derali, Emmanuel Kamwendo akuti vuto ndi phungu yemwe sakumuyendera komanso wati kusowekera kwa njinga zamoto zomwe adawalonjeza ndi vuto lina.
Ngati ndayendera wodi yanga ndiye kuti ndatengedwa ndi abungwe apo ayi sizitheka. Npake kuti anthu ayambe kudandaula kuti sindikuwayendera, adatero Kamwendo.
Nako ku Karonga malinga ndi Senior Chief Kalonga yati ntchito yangoyamba kumene.
Dzulo [pa 23] kudali nkhumano ya makhansala kukambirana momwe angamapezere ndalama zotukulira khonsolo ino. Ngati ndaona ntchito ndi imeneyi, adatero Kalonga.
Mkulu wa bungwe lomwe ntchito zake ndikutukula anthu akumudzi la Miglat lomwe pano likugwira ntchito zake mboma la Chiradzulu ndi Thyolo, Victor Mkolongo akuti mmaboma amene akugwira ntchitowa makhansala ayamba bwino ntchito yawo ngakhale patenga nthawi.
Msabata yomweyi makhala onse 10 a mboma la Chiradzulu adatiyendera kuti aone ntchito zathu. Aka ndikoyamba kuyenderedwa komanso ndikumva kuti kuyenda kwawo koyamba chisankhidwireni ndikumeneku. Tingati ayamba bwino ngakhale zatenga miyezi kuti ayambe kugwira ntchitoyi, adatero Mkolongo.
Naye Jephter Mwanza yemwe amachita mapologalamu a Kalondolondo akuti ngakhale nthawiyi yachepa chisankhidwireni komabe zikuonetsa kuti pali mavuto ndi ntchito zawo.
Ndinali ku Nsanje, ena akuoneka kuti sakudziwa ntchito yawo pamee ena akuoneka kuti akuzitsata. Nkhani yakula mkusiyanitsa ntchito za khansala ndi phungu, adatero Mwanza.
| 11 |
Chipatala chidzapulumutsa K730m pachaka Chipatala cha khansa chomwe boma likumanga ku Lilongwe chikatsegulidwa mwezi wa September chaka chino, boma kudzera ku Unduna wa Zaumoyo lizipulumutsa K730 miliyoni pa chaka.
Ndalamazi ndi zomwe boma limagwiritsa ntchito potumiza anthu odwala khansa kunja kukalandira thandizo lomwe tsopano lizipezeka mdziko Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka momwemuno kudzera kuchipatalachi.
Mkulu wa bungwe loona zaumoyo la Malawi Health Equity Network (Mhen), George Jobe, wati iyi ndinkhani yabwino chifukwa Unduna wa Zaumoyo uzigwiritsa ntchito ndalamazi pa zinthu zina zofunikira monga kugula mankhwala ndi mafuta othira mmaambulasi.
K730 miliyoni ndi ndalama zambiri zedi zoti kuzigwiritsa ntchito bwino zikhoza kupindulira anthu ambiri ku ntchito ya zaumoyo. Monga tikudziwa, mafuta a ambulansi ngakhalenso mankhwala zimasowa, adatero Jobe.
Unduna wa zaumoyo wati chiwerengero cha anthu omwe ali ndi khansa chodziwika mdziko muno ndi 15 000 ndipo boma limatumiza anthu 40 mwa anthuwa kunja kukalandira thandizo la mankhwala ndipo munthu mmodzi amafunika K22 miliyoni kuti apite kunja, akalandire thandizo nkubwerako.
Bungwe loona za anthu odwala ndi khansa la Cancer Association of Malawi lati thandizo lomwe odwala khansa amalandira kuchipatala cha Gulupu ku Blantyre ndi loperewera ngakhale kuli mpumulo pangono.
Mkulu wa bungwelo, Regina Njirima adati khansa imafunika chipatala chakechake chifukwa anthu odwala khansa amafunika kuonedwa pafupipafupi komanso kuwasakaniza ndi anthu odwala matenda ena kumawapangitsa kudzimvera chisoni kwambiri.
Wodwala khansa amakhala ndi nkhawa zambiri kotero amafunika pamalo oti nkhawazo zizichepa. Njira yabwino nkukhala ndi chipatala chawochawo chomwe chili ndi zipangizo komanso akadaulo othandiza odwalawo adatero Njirima.
Mmodzi mwa anthu omwe adadwalapo khansa ndipo adachira atapita kuchipatala Janet Bonwel a kwa T/A Ndindi ku Salima adati kupeza thandizo la khansa Mmalawi nkovuta moti anthu ambiri akuvutika ndi matendawa.
Iye wati adapezeka ndi khansa ya mmwendo mu 2001 ndipo kuzipatala zosiyanasiyana komwe amapita amangopatsidwa Panado yemwe samachotsa nkomwe ululu omwe adali nawo.
Iye wati adakapeza thandizo kuchipatala cha Ndimoyo ku Salima komweko.
Ululu wa khansa siwamasewera. Ndidachita kusiya kugwira ntchito iliyonse ndipo sindimatha kugona chifukwa chaululu kumangobuula usiku ndi usana. Ndidalowera uku ndi uko koma osapeza thandizo mpaka ndidafika potaya mtima kuti ndizingodikira imfa, adatero Bonwel.
Iye wati chipatala cha khansa chibweretsa mpumulo waukulu kwa anthu omwe ali ndi khansa.
| 2 |
Chisankho chiliko Bwalo lalikulu la milandu la Supreme Court dzulo lidagamula kuti bwalo lapadera la Constitutional Court (ConCourt) silidalakwe pogamula kuti chisankho cha pa 21 May 2019 sichidayende bwino.
Choncho, chisankho cha mtsogoleri wa dziko lino chichitikabe pa 2 July 2020. Ndipo bwalolo lati okhawo amene adalembetsa pa mavoti a 2019 ndiwo adzavotenso, osati amene amalowa mkaundula watsopano amene wakhala akuchitika.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Nyirenda: Chisankho si chibwana Lazarus Chakwera yemwe adaimira chipani cha Malawi Congress Party (MCP) ndi Saulos Chilima yemwe adaimira UTM Party adakamangala kukhoti kuti bungwe la zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) silidayendetse bwino chisankhocho polengeza kuti mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika ndiye adapambana pachisankhocho.
Pa 3 February chaka chino lidagamula kuti chisankhocho sichidayende bwino ndipo pakhale chisankho china pasanathe masiku 150. Bwalolo lidagamulanso kuti Nyumba ya Malamulo iunike momwe makomishona a MEC adayendetsera chisankhocho. Aphunguwo adapempha Mutharika kuti achotse makomishonawo, limodzi ndi wapampando akuimalimodzi ndi Muluzi yemwe akudziwa bwino za chitukuko.
Polankhula ndi opereka zikalatazo payekhapayekha, wapampando wa MEC Jane Ansah adati pochita kampeni, atsogoleriwo ayenera kubwera ndi njira zatsopano zochitira kampeni. Malinga ndi matenda a Covid-19, boma lidati anthu asakhale oposa 100 malo amodzi, zimene zingakhudze kampeni yomwe idayamba pa 2 May.
Padakalipano, akadaulo a za ndale ena aikapo mlomo pa momwe chisankhochi chikuyendera.
Ndipo kadaulo wina, Humphreys Mvula adachenjeza kuti ngakhale mwayi iye adakana kuchotsa makomishonawo.wawo Jane Ansah, koma Koma, mchigamulo chawo, oweruza 7 a Supreme Court adadabwa chifukwa chomwe MEC ndi Mutharika adachitira apilo alibe mfundo zokwanira.
Mkulu wa oweruzawo, Andrew Nyirenda adati mwa mfundo 137 zimene zidaperekedwa pochita apilo, zidali zokolana, zongobwereza, zosatsata ukadaulo wa zamalamulo komanso zochititsa manyazi.
Nyirenda adati: Chisankho ndi nsanamira ya demokalase chifukwa kumakhala kusankha atsogoleri. Si zinthu za masewera. Chisankho chiyenera kuyenda mwa chilungamo osati mongawaula kuti pachitika chisankho.
Mchigamulocho, oweruza adati MEC idaphwanya malamulo a dziko pakayendetsedwe ka chisankhocho.
| 11 |
Kalikiliki popewa ngozi za madzi Pamene nkhani yolosera mvula ili mkamwamkamwa, boma lati lili pakalikiliki kuti madzi osefukira amene amasautsa mmadera ena chaka chino lisakhale vuto la mnanu.
Ambiri mwa anthu omwe amakhudzidwa ndi omwe amakhala mmphepete mwa madzi makamaka mmaboma a kuchigwa cha Shire: Chikwawa ndi Nsanje. Chaka chatha kusefukira kwa madzi kudankitsa ndipo kudakhudza maboma 18 mdziko muno, mpaka mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika adati dziko lino ndi la ngozi, zimene zidachititsa kuti mabungwe ndi maiko athandizepo.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Malinga ndi mkulu wa nthambi yoona ngozi za dzidzidzi Bernard Sande, chomvetsa chisoni nchakuti ngozi zotere zikachitika boma limaononga ndalama za nkhaninkhani kusamala anthu okhudzidwawo ndi kubwezeretsa zinthu zoonongeka.
Chaka chino chokha boma lidati likufunika K215 biliyoni zoti likonzetsere zinthu zomwe zidaonongeka ndi madzi osefukira dzinja lathali pomwe anthu, ziweto ndi katundu wawo zidakokoloka.
Zambiri mwa zofunika kukonzedwazo ndi milatho, masukulu, misewu, zipatala ndi zogwiritsa ntchito mmalowa zomwe zidaonongeka.
Sande adati chomvetsa chisoni nchakuti anthu omwe amakhudzidwa kawirikawiri amakakamira kukhala kumadzi komwe sikuchedwa kusefukira ndipo adati chaka chino boma likufuna anthu onse okhala mmalo oterewa achokeretu mvula isadayambe.
Tayamba kale kulangiza anthu kuti achoke mmadera momwe mumasefukira madzi ndipo tionetsetsa kuti onse achoka chifukwa sitikufuna kuti chaka cha mawa tizidzakambanso nkhani yomweyi, adatero Sande.
Iye adati anthuwa amati sangachoke mmalomo chifukwa makolo awo adamwalira ndi kuikidwa momwemo komanso malo olima ndi kuweterapo ziweto zawo ali momwemo.
Malinga ndi T/A Maseya ya mboma la Chikwawa, anthu amavuta pankhani yamalo chifukwa amakhulupirira kuti kusiya malo omwe padagona mizimu ya makolo awo kuli ngati kuwagalukira nchifukwa chake safuna kusamuka.
Iye adati vuto lina ndi lakuti malo omwe anthuwo amakhala ndi aakulu kutanthauza kuti atati asuntha ndiye kuti komwe angapiteko malo sangakawakwanire potengera pokhala ndi polima pomwe.
Kupatula kukhulupirira kukhala pamodzi ndi mizimu ya makolo awo, vuto lina ndi malo okhalapo ndi kulima kumtundako, adatero Maseya.
Paramount Kyungu ya ku Karonga adagwirizana ndi Sande pankhaniyo ndipo adati palibe phindu kutaya moyo chifukwa chokakamira manda ndi minda mmalo mosuntha kupita kumtunda ndi kudzabwerera mchilimwe.
| 5 |
Amangidwa kaamba kobisa khanda Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Pamene amayi ena akukangana ndi amuna awo mmidzimu kufuna nsalu yalekaleka, amayi ena ndi pamene mwayi woterewu akumauseweretsa nkumataya ana oberekabereka nkuthiridwa maunyolo ndi apolisi.
Izi zikutsatira kumangidwa ndi kutsekeredwa mchitolokosi kwa mayi wa zaka 22 pomuganizira kuti adafuna kubisa khanda lomwe adabereka ku Dowa.
Wofalitsa nkhani za polisi mboma la Dowa, Richard Kaponda, wati mayiyu ndi Jenifer Wilson, wa mmudzi mwa Kamphelo mdera la T/A Mkukula mbomali.
Kaponda adati nkhaniyi idachitika pa 4 August chaka chino mmudzi mwa Kamphelo.
Nkhani, Malingana ndi Kaponda, ikuti mayiyu ankakhala ku Lilongwe ndi chemwali wake wamkulu ndipo ali komweko mwamuna wina adamuchimwitsa ndi kumupatsa pathupi.
Iye adaganiza zopita kwa makolo ake ku Dowa atalephera kuchotsa pakatipo ndipo atafika kumeneko sadadziwitse makolo ake za nkhaniyi ndipo amaphimba mimbayo kuti isaonekere kunja ndi anthu.
Pomwe nthawi idakwana yoti abereke, adapita pathengo lina loyandikira pomwe padali chulu ndipo adabereka mwana wamkazi koma adamutayira mdzenje pachulupo momwe munali chiswe chomwe chinayamba kuteketa mwanayo, adafotokoza Kaponda.
Iye adati khandalo lidayamba kulira ndipo anthu amene ankadutsa pafupi ndi chulucho ndi amene adamva kulirako ndipo adakatsina khutu mfumu ya mmudzimo, yomwe idakanena kwa apolisi.
Kaponda adafotokoza kuti mwanayo adamutengera kuchipatala chachikulu cha Dowa komwe adakamwalira ndi chibayo kaamba kozizira.
Mayiyu woganiziridwayu adamumanga kaamba koti amatulutsa magazi atakamupima kuchipatala, zomwe zidapangitsa amuganizire kuti adabereka ndi kutaya khanda lake mdzenjemo.
Mayiyu akuyembekezereka kukaonekera kubwalo la milandu posachedwapa komwe akayankhe mlandu wofuna kubisa khanda.
| 7 |
Mwambo wogwetsa simba Sukulu zatsekera ndipo zikatere mmaboma ambiri makolo ali kalikiriki kukonzekera kuti ana awo apite kusimba kukavinidwa. Kumenekotu kumakhala uphungu kuti anawa adziwe khalidwe komanso momwe zina za mbanja zimakhalira. Zambiri zakhala zikukambidwa zokhudza unamwaliwu koma sabata ino BOBBY KABANGO akutibweretsera mwambo womwe umachitika pamene anamwali akutulutsidwa kusimba pachinamwali cha jando. Kodi zimakhala bwanji? Tidziwane Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Ndine Evason Chalamanda, wamkulu wa simba muno mmudzi mwa Malika, kwa T/A Mpama mboma la Chiradzulu. Ngati mukufuna kudziwa chilichonse cha simba, ine ndiye mwini wake.
Timamva kuti kumakhala mwambo patsiku lomwe mukusasula simba, kodi ndi zoona? Zimenezo ndi zoonadi, chinamwali ndi mwambo ndiye pamene mwamaliza kulanga anamwali, mumayeneranso kuti mutsate mwambo womwewo ngati mukusasula simba. Ndigwirizane nanu kutidi pamakhala mwambo.
Umakhala mwambo wanji? Mwambo wosangalala basi, kuti tamaliza chinamwali. Tikawasunga anamwaliwa kwa sabata zitatu, ndiye tsiku lomwe tikuwatulutsa timayenera kukhala ndi mwambo basi.
Mwambowo umachitikira kuti? Malo alionse oyandikana ndi simbalo koma usachitikire kunyumba. Mumangotuluka kusimbako ndi kukhala chapafupi ndi simbalo. Mwambowu suchitikira kusimba chifukwa kumakhalabe anamwali. Dziwani kuti mwambowu ukamayambika anamwali amakhala asanatulutsidwe ndipo amadzakupezani mwambowo uli mkati. Komanso dziwani kuti amayi ndi anthu amene sadavinidwe sayenera kufika kusimbako nchifukwa mwambowo suchitikira kumeneko.
Bwanji osangopangira kusimba komweko? Pamene tikusasula simba, timafuna tisangalale ndi anzathu. Makolo, achibale komanso anzathu kuchokera midzi yosiyanasiyana amabwera. Poti anthuwa saloledwa kufika kusimba, nchifukwa chake timachoka kusimbako kuti tikumane malo abwino. Anthuwa amakhala akufupa anamwaliwa pamene atuluka kusimbako.
Kodi kumakhala zochitika zotani patsikuli? Aliyense amachita monga akufunira koma kunoko timakhala ndi mwambo wosangalala ndi magule, timakhala ndi azungu komanso chinyama zomwe zimasangalatsa anthu amene abwera kudzaonerera mwambowo.
Azungu? Eya, kapena kunena kuti anthu amene khungu lawo ndi loyera.
Amachokera kuti? Amachokera kusimba komweko! Ndi a mdziko lomwe lino? Kapena mumachita kupangatu inu Ndi anthu amene amakhala kusimbako koma amakhala kuti adavinidwa kale. Awa si anamwali chifukwa anamwali amatuluka usiku basi, pamenenso kumakhala mwambo wina.
Kodi ndi azungudi? Kapena mundipusitsatu Amenewa si azungu enieni, timachita kupanga kusimba komweko. Timatenga dothi nkuliviika mmadzi. Likafewa timawauza kuti ayambe kudzola thupi lonse ndipo likauma munthuyo amafanana ndi mzungudi.
Amaoneka bwanji? Khungu ngati mzungu, koma mavalidwe ndiye amavala zosiyasiyana chifukwa ena amavala nsalu, ena dilesi ndiye amaoneka ngati atsikana koma onse ndi anyamata.
Ndiye mwati kumabweranso chinyama? Eya ndipo chimakhala chofanana ndi mbalame. Dzina lake timachitcha chimwanambera. Ntchito yake nkuopseza ana kuti adziwe za kuopsa kwa samba. Paja ndanena kuti kumabweranso ana koma sikuti chimawamenya.
Mumachitanso kupanga? Eya, timachipanga ndi mitengo, kunjako timachikutira ndi bulangete kapena nsalu. Mkatimo mumakhala anthu awiri kapena mmodzi kuti azichiyendetsa.
| 18 |
Akagwira Ukayidi Zaka Ziwiri Kamba Kopezeka Ndi Chamba Bwalo loyamba la milandu (First Grade Magistrate) mboma la Mangochi lalamula bambo wina wa zaka 49 zakubadwa kuti akakhale ku ndende ndi kukagwira ntchito ya kalavulagaga kwa zaka ziwiri ndi miyezi inayi kamba kopezeka ndi chamba zomwe ndi zotsutsana ndi gawo 4 la malamulo oweruzira milandu mdziko muno.
Pofotokozera bwalolo, yemwe amayimira boma pa mlanduwu ku bwaloli Superintendent Davison Banda anati munthu wina wakufuna kwabwino ndi yemwe anatsina khutu apolisi kuti bambo-yu Mariyo Makweche amapezeka ndi chamba, ndipo apolisi-wa atakachita chipikisheni ku nyumba ya mkuluyi ndi komwe anakapezadi chamba chomwe chinali cholemera makilogram 114.
Koma a Makweche atafunsidwa za za mlandu-wu akuti anauvomera ndipo anapempha bwalolo kuti liwapatse chilango chofewa kamba koti amayanganira banja lawo.
Popereka chigamulo First Grade Magistrate, Roy Kakutu analamula bambo-yu kuti akagwire ukayidi wa kalavula gaga kwa zaka ziwiri ndi miyezi 4 kuti ena atengerepo phunziro.
A Mariyo Makweche amachokera mmudzi mwa Chimesya mdera la mfumu yaikulu Chowe mboma la Mangochi.
| 7 |
Mpingo ukana mbusa womangidwa za zitupa Mpingo wa Lords Chosen Charismatic Revival Ministries (LCCRM) wakana zomwe munthu wina wa ku Cameroon adauza nthambi yoona za anthu olowa ndi kutuluka mdziko muno kuti iye ndi mbusa komanso mtsogolera wa mpingowu mdziko muno.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Abusa ndi Akhrisitu a mpingowu ati Israel Ejelli adachoka mumpingowo iwo atapempha a kulikulu lawo ku Nigeria kuti amuchotse patchalitchipo chifukwa chosasangalala ndi zomwe amachita.
Mmodzi mwa abusa akuluakulu a mumpingowu Desmond Ugochukwu wa ku Nigeria wati Ejelli anali mkulu wa mpingowu kuno ku Malawi koma ankachita zosemphana ndi malamulo a mpingowu komanso sankalemekeza mtsogoleri wa mpingowu.
Vuto lenileni lomwe anali nalo ndi lakuti amaderera mtsogoleri wa mpingo wathu dziko lonse, mbusa Lazarus Muoka, yemwe ali ku Nigeria komanso amaphwanya malamulo a mpingo wathu, adatero Ugochukwu.
Iye wati mpingowu udaganiza zoyamba kumusala ndipo likulu la mpingowu lidatumiza mbusa wina Peter Ndukwe wochokeranso ku Nigeria kuti adzatenge udindo wotsogolera mpingowu.
Ugochukwu akuti mbusa wokanidwayo ataona kuti sakugwirizana ndi Akhristu a mumpingowo adapempha kulikulu kuti akufuna kuchoka mumpingowo ndipo adamulembera kalata yomuvomereza kuchokako yomwe adadzaipereka kutchalitchiko.
Mmabuku mwathu tikudziwa zoti adatuluka mumpingo ndipo si mbusanso koma tikudabwa kuti akumagwiritsa ntchito mpingowu ngati chizindikiro chake. Posachedwapa atamangidwa adauza apolisi kuti ndi mtsogoleri wa mpingo uno chonsecho adapuma ndipo mtsogoleri panopa ndi mbusa Peter Ndukwe.
Zimenezi zakwiyitsa Akhristu athu ndipo tikhala pansi kuti tione chomwe tingachite asanapitirize kuononga mbiri ya mpingo, adatero Ugochukwu.
Mneneri wa nthambi yoona za anthu olowa ndi kutuluka mdziko muno kuofesi ya ku Lilongwe, Ealack Banda, adati Ejelli adamangidwa pamlandu wopanga ziphaso zachinyengo.
Iye adati nkhaniyi idaphulika akuofesi ya kazembe wa dziko la China atauza nthambiyi kuti munthu wina adapita kuofesiko ndi ziphaso zinayi zachinyengo zomwe ankafuna kutengera zilolezo za anthu ena a ku Ghana.
Titamva izi tidamanga munthuyo, Daniel Bart-Plange, wa zaka 32, koma titafufuza nkhaniyi idakhudzanso mbusayo [Ejelli] ndipo tidawamanga, adatero Banda.
Akuluakulu a mpingowu ati kalata zomwe mpingowo udamupangitsira Ejelli kuti adzagwire ntchito ngati mbusa kuno ku Malawi zidatha ntchito.
Mpingowu akuti udabwera kuno ku Malawi mu 2003 ndipo uli ndi nthambi ku Lilongwe ku Area 2 ndi ku Mzuzu.
Banda wati Ejelli anamutulutsa pabelo ndipo akuti azikaonekera ku ofesi yowona za anthu olowa ndi kutuluka mdziko muno Lolemba lililonse pomwe mnzakeyo, Bart-Plange, ali kundende ya Maula koma onse akudikira tsiku la mlandu.
Tidalephera kulankhula ndi Ejelli chifukwa samadziwika kumene akukhala.
Awiriwa akadzapezeka olakwa adzamangidwa ndi kukagwira ntchito ya kalavula gaga kwa zaka zitatu chifukwa chophwanya gawo 356 la malamulo a dziko lino.
| 13 |
Malawi ali mumdima wa dzaoneni Dziko la Malawi laona mdima womwe sudaonekepo chilandirireni ufulu wodziyimira palokha. Madera ena akukhala masiku awiri magetsi osayaka. Kwina, ndiye mpaka kumatha masiku atatu. Akangoyaka, pena sakumatha ola upeza azima kale.
Ophunzira, eni makampani, zipatala, komanso zigayo akubuula mumdima wa ndiweyani. Chipulumutso sakuchiona. Ngakhale zikumveka kuti kukubwera majeneleta, Amalawi akuda nkhawa chifukwa mitengo ya magetsi nawo akuti idzakwera. Mtendere sukudziwika tsiku lomwe ukudza.
| 10 |
Mtima pansi, mayeso A jce alipo chaka chino Ngati panali kupeneka kulikonse kuti chaka cha 2015/16 kukhala kapena sikukhala mayeso a Junior Certificate of Education (JCE) kutsatira zomwe boma lidalengeza posachepadwa kuti lathetsa mayesowo msukulu za sekondale, kukaikako kutheretu chifukwa boma latsimikiza kuti mayesowo alembedwa.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Escom in free-for-all fuel scam Eni sukulu zomwe si zaboma akhala akudandaula kuti boma lawaika pachingwe cha kangaude polephera kubwera poyera ndi kufotokoza ngati mayesowo aliko kapena ayi zitangomveka kuti boma lathetsa satifiketi ya JCE, koma osamasula kuti zimenezi ziyamba liti.
Ophunzira kulemba mayeso a JCE mmbuyomu Mneneri wa unduna wa zamaphunziro, Manfred Ndovi, wati pasakhale mpungwepungwe uliwonse pankhaniyi poti mayesowa aliko koma kuyambira chaka cha mawa cha 2017 mayesowa sadzalembedwanso.
Mayeso aliko! Chaka chino chikhala chomaliza kulembetsa mayeso a JCE koma kuyambira chaka cha 2017 sikudzakhalanso mayeso oterewa, adatero Ndovi pouza Tamvani palamya.
Iye adati sukulu ndi ana onse omwe ali Fomu 2 ndipo akuyembekezera kulemba mayeso a JCE, atsatire ndondomeko zonse zoyenerera pokonzekera mayesowa, osati kutekeseka.
Mkulu wa bungwe la eni sukulu zomwe si zaboma, Joseph Patel, adauza Tamvani kumayambiriro a sabatayi kuti eni sukuluzi akusowa kolowera pankhaniyi kaamba kakuti sakudziwa ngati mayesowa alembedwe chaka chino kapena ayi.
Boma lidaganiza zoyambitsa njira yosefera ophunzira potengera momwe akuchitira mkalasi komanso pamayeso a teremu iliyonse mmakalasi onse kulekeza Fomu 3 kuti Fomu 4 ndiyo azilemba mayeso a boma.
Pofotokoza mmene zizidzayendera, nduna ya zamaphunziro, Dr Emmanuel Fabiano, idauza Tamvani kuti ndondomeko yatsopanoyi ikadzayamba bungwe la Maneb lidzasamba mmanja pachilichonse chokhudza JCE ndipo malo olemberamo mayeso (cluster centres) ndiwo adzasenze udindo.
Ndondomeko idzakhala yakuti malo olemberamo mayeso ndi ana omwe akuyenera kulemba mayeso azidzalipira ndalama za mayeso ku cluster yomwe izidzakonza mayeso ndi kulembetsa, adatero Fabiano.
Ndunayi idati sipadzakhala zobwereza kalasi kapena kuchotsedwaokhoza ndi olakwa omwe azidzapitirira mpaka mu Fomu 3.
Fabiano adati boma lagani izi pofuna kupereka mpata kwa ophunzira onse omaliza nawo maphunziro a kusekondale komwe akalemba mayeso a Fomu 4, okhoza azidzapatsidwa satifiketi ya MSCE pomwe olakwa azidzalandira kalata yaumboni yoti adamaliza maphunziro a kusekondale.
Iye adati izi zizichititsa kuti ambiri azilandira nawo maphunziro okwanira chifukwa mundondomeko yakale, olakwa JCE amachoka pasukulu ndipo ambiri sankakhalanso ndi chidwi chokapitiriza kwina.
Mfundo ya boma pochotsa mayeso a JCE ndi yakuti satifiketiyi idatha mphamvu chifukwa olemba ntchito ambiri masiku ano safuna satifiketiyi koma yokwererapo.
| 3 |
Ziyaye Alimbitsa Akhristu 345 ku Parishi ya Likuni Wolemba: Sylvester Kasitomu Episcope wa Arch-Diocese ya Lilongwe ambuye Tarsizio Ziyaye lamulungu walangiza ankhristu mu Archi-Dayosiziyi kuti agwiritse bwino ntchito mphatso za Mzimu Woyera pa kudzamitsa moyo wa Uzimu pakati pawo.
Ambuye Ziyaye amalakhula izi lamulungu ku Parish ya Holy Rosary-Likuni pa mwambo wopereka Sacrament la Ulimbitso.
Iwo anati akhristu amalandila mphatso zimene mulungu mzimu woyera amapereka komanso kutumidwa ndi yesukhristu kuti akalalike nthenga wambwino kudzera mu sacramentili.
Sacrament la ulimbitso lili mu guru la masacrament oyambilira amene ndi ofunika kwambiri ndipo kudzera mu sacrament ili mulungu mzimu woyera amatituma ndikutipatsa mpatso zake kuti tikhale mboni za yesu khristu, anatero Ambuye Ziyaye.
| 13 |
Dziko layaka moto, Bushiri wachenjeza Mneneri wa mpingo wa Enlightened Christian Gathering (ECG) Shepherd Bushiri wachenjeza atsogoleri andale kuti mpungwepungwe womwe uli mdziko muno utha kudzetsa mavuto a akulu.
Bushiri, yemwe amakhala ku South Africa, wapempha atsogoleriwo kuti akonzekeretse anthu awo kudzavomera zotsatira za mlandu wa chisankho cha mtsogoleri wa dziko lino womwe uli ku khoti.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Kudali mkokemkoke ku Lilongwe Lachiwiri, anthu okwiya atatseka misewu ndi matayala a moto Zipani za Malawi Congress Party (MCP) ndi UTM zidakokera ku khoti chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) ndi bungwe la Malawi Electoral Commission powaganizira kuti adabera chisankho cha mtsogoleri wa dziko lino.
Bushiri adati kupanda kukonzekeretsa anthu kudzalandira chigamulo cha khoti kutha kudzaonongetsa katundu wambiri kuposa yemwe waonongeka kale.
Zinthu zambiri zaonongeka kaamba ka zionetsero zomwe zakhala zikuchitika mdziko muno pofuna kukakamiza wapampando wa MEC Jane Ansah kuti atule pansi udindo wake pomuganizira kuti sadayendetse bwino zisankho zapatatu za pa May 21.
Bungwe la Human Rights Defenders Coaliation (HRDC) ndilo likutsogolera zionetserozo.
Ansah adakana kutula pansi udindo wake zomwe zachititsa kuti HRDC ipitirize kuchita zionetsero.
Bushiri adati zionetserozi zaonetsa kale Amalawi mbwadza, koma zenizeni zazikulu zikubwera ngati anthu sadzavomereza zotsatira za mlanduwo.
Anthu akutaya miyoyo. Posachedwapa mnyamata wamphamvu zake ku Karonga adataya moyo wake mdzina la zionetsero.
Anthu akumenyedwa nkumasiyidwa atatsala pangono kufa chifukwa amachokera mchigawo china kapena amatsatira chipani china ndipo atsogoleri athu akuoneka kuti sakufuna kugwirizana, iye adatero.
Bushiri adati sakudana ndi zionetsero chifukwa ndi ufulu wa anthu kutero, koma chomwe akudana nacho ndi zipolowe zomwe zionetsero zikudzetsa.
Iye adati ndiwokonzeka kukhala mkhalapakati wa mbali zonse zomwe sizikumvana pa nkhani ya chisankho cha pa May 21 2019.
Mneneri wa MCP Maurice Munthali adati za mtendere si zachilendo mu chipani chake.
Iye adati zomwe Bushiri akunena ndi zomwe mtsogoleri wa chipanicho Lazarus Chakwera amafotokozera otsatira ake. Mneneri wa chipani cha DPP Nicholas Dausi adangoti chipani chawo ndi +cha mtendere, koma sadathirirepo ndemanga pa zomwe Bushiri adalankhula.
| 13 |
Adzudzula JB zomanga mfumu Nkhata: Nzodabwitsa Mphunzitsi wa za malamulo kusukulu yaukachenjede ya Chancellor College Mwiza Nkhata wati ndi zodabwitsa kuti mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda walamula apolisi kuti anjate T/A Chimombo ya ku Nsanje.
Nkhata wati ngakhale pulezidenti ndi komanda wa asilikali ndi apolisi, sakuyenera kutero chifukwa kunjata munthu kumafunika kufufuzidwa kaye kunjatako kusadachitike.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Banda Lachiwiri adalamula apolisi kuti anjate Chimombo pomuganizira kuti adasowetsa chigayo chomwe chidaperekedwa mu 2008 kuti chithandize olumala.
Ndikulamula kuti wachiwiri kwa pulezidenti [Khumbo Kachali] alowererepo pankhaniyi mpaka wokhudzidwayo atamangidwa, adatero Banda.
Koma Nkhata akuti pali zambiri zomwe Banda akadachita asadalankhule mawu akewo.
Kumanga kuli mmanja mwa apolisi, atha kuuza mkulu wa apolisi kuti afufuze nkhaniyo kapena kuchita chilichonse koma kufika polamula chonchi ndi zachilendo.
Apolisi amayamba afufuza kaye asadanjate munthu, tsono akalamula kuti amangidwe kodi amumanga chifukwa wina walamula kapena apeza zifukwa zomumangirazo? adatero Nkhata.
Mneneri wapolisi ya Nsanje Samson Balakasi Lachinayi adati mfumuyo siidanjatidwe. Pofika Lachisanu madzulo tikhala titafika pena pake ndi nkhaniyi, adalonjeza Balakasi.
Mfumuyi yomwe dzina lenileni ndi Stanford Ntukula idaimitsidwa pa ntchito yake chaka chatha kuti ifufuzidwe za malipoti oti amachitira nkhanza anthu ake.
Anthu a mderalo adakamangala kupolisi sabata yatha kuti afufuze za chigayocho.
| 8 |
Zig Zero: Mnyamata wa nyimbo za dansi Kuyambira kuubwana wake chimene amaganiza, kulota ndi kuchita ndi kuimba nyimbo basi. Inde, Mulungu adamudalitsa ndi liwu lanthetemya mnyamata ameneyu ndipo pano akugwiritsa ntchito luntha lomwelo kuti apeze chakudya cha tsiku ndi tsiku komanso zosowa pamoyo wake. Uyu ndi Joseph Alufandika, mnyamata wosangalatsa anthu ndi mingoli yokoma. CHIMWEMWE SEFASI adapezana naye poduka mphepo ndipo adacheza naye motere: Kudyera pakamwa: Alufandika Ndikudziwe Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Dzina langa ndine Joseph Alufandika, ndipo ndine wosakwatira, ndimachokera kuchigawo chakumwera konkuno mboma la Nsanje. Anthu okonda nyimbo za dansi amandidziwa ndi dzina loti Zig Zero.
Kodi kuimba nyimbo za dansi udayamba liti? Kuimba ndidayamba pakale ndithu. Ndili kusekondale ndi pamene ndidazindikira kuti ndili ndi luso losangalatsa anthu kudzera mumaimbidwe, munyimbo za dansi.
Kodi kupatula kuimba umachitanso chiyani? Inetu ndimapanga bizinesi komanso ndikupitiriza maphunziro kusukulu ya Malawi College of Accountancy komwe ndikuphunzira zoonkhetsa chuma.
Kodi chimbale chako chatsopano chituluka liti? Mutu wake ndi chiyani? Chimbale changa chikuyembezereka kutuka kumapeto a mwezi wa August, chomwe chikhale ndi nyimbo 14 zomwe zaimbidwa mChichewa ndi mChingerezi. Ndipo kuyambira pa 3 August mpomwe nditawadziwitse Amalawi zambiri.
Kodi ndi mavuto ati omwe oimba nyimbo za dansinu mumakumana nawo? Mavuto omwe timakumana nawo ndi monga kupita kuzoimbaimba koma osapatsidwa ndalama yomwe tinagwiriza. Kumeneku ife timaona ngati tikuponderezedwa komanso anthu ena kuti atukule luso lathu amafuna kuti tiwapatse ndalama.
Kodi nyimbo za dansi ngati zomwe umaimba iweyo ukuona kuti zikupita patsogolo? Kunena mosanama, Chimwemwe uli apa, nyimbo zaimbidwa ndi achinyamata zikupita patsogolo kwambiri chifukwa anthu akati ali pamalo achisangalalo monga kuukwati, zinkhoswe, malo osiyanasiyana, chisangalalo chawo chimakhala chopambana chifukwa cha uthenga womwe tikumapereka kudzera mnyimbo zomwe tikumawapatsira .
Kodi ndi anthu ati omwe unaimbapo nawo nyimbo limodzi chiyambireni kuimba pa Malawi pano? Inetu chiyambireni kuyimba pa Malawi pano ndaimbapo nyimbo ndi anthu ambiri monga Marcus Pasanje wa Dare Devils, Blasto, BFB ndi ena ambiri.
Pomaliza tandiuze zomwe umakonda.
Ine ndimakonda kuimba ndi kumvera nyimbo. Nthawi zina ndimakonda kuyenda ndi kumaona malo osiyanasiyana ndi kukumana ndi anthu osiyanasiyananso.
| 9 |
Papa Wapempha Akayidi Alimbikitse Makhalidwe Abwino Wolemba: Thokozani Chapola Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco wapempha akayidi mu ndende zosiyanasiyana pa dziko lonse kuti akatuluka mu ndende-zi azikalimbikitsa makhalidwe abwino.
Papa pa umodzi mwa maulendo ake oyendera akayidi Papa amalankhula izi pomwe amakumana ndi mamembala a bungwe lomwe limadzipereka pa ntchito zosamalira akayidi mu ndende, atangomaliza msonkhano wawo kulikulu la mpingo-wu ku Vatican.
Msonkhanowu unachitika kuyambirapa 7 ndi kutha 8 mwezi uno. Mwazina mthumwi zimakambirana mfundo zikuluzikulu zothandiza pa ntchito zokweza bungwe-li.
Pamenepa Papa Francisco, anathokozanso mamembala a bungweli kamba kodzipereka pa ntchito zosamalira akayidi mu ndende zosiyanasiyana.
| 13 |
Anthu Ayembekezere Kusintha pa Ntchito Zofalitsa Nkhani-Kazako Boma lati nyumba zofalitsa nkhani mdziko muno ziyembekezere kusintha kwakukulu pa kagwiridwe ka ntchito zake komanso pa miyoyo ya atolankhani.
Kazako: Anthu anavota kuti zinthu zisinthe Nduna ya zofalitsa nkhani a Gospel Kazako ndi omwe anena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi.
Iwo ati kusinthaku kufikiranso magulu ena a wanthu omwe ali mu gawo la zofalitsa nkhani komanso kutumiza mauthenga zomwe pamapeto pake zisintha miyoyo ya mzika za dziko lino.
Anthu mdziko muno anavota kuti zinthu zisinthe ndiye kusintha kumeneku kuchitika pakati pa a Malawi kuphatikizapo atolankhani komanso mmene nyumba zowulutsamawu zizigwilira ntchito.
Zimenezi zikhudzanso anzathu a lamya za mmanja komanso othandiza potumiza mauthenga. Kusintha kumeneku pamapeto pake kukhala kokomera anthu onse mdziko muno, anatero a Kazako.
Pamene amalankhulapo za udindo wawo nduna yatsopanoyi yati idalira chithandizo cha Mulungu kuti igwire bwino ncthito zake pa udindowu.
| 14 |
Afa Atawombedwa ndi Mphenzi ku Nkhotakota Mamuna wina wa zaka 32 zakubadwa wafa mboma la Nkhotakota mphezi itamuwomba akuwedza nsomba pa Dziwe la Chia Lagoon.
Nkhalamo anagwera pa damu limeneli Wofalitsa nkhani za apolisi mbomalo, Sub Inspector Williams Kaponda wati mamuna womwalirayu yemwe amadziwika ndi dzina loti Sweet Nkhalamo adali ndi anzake ena awiri kowedza nsomba ku Chia Lagoon pa 30 December 2019.
Mwadzidzidzi mvula idayamba kugwa ndipo mphezi idawawomba atatuwa ndipo adagwera mmadzi, koma chifukwa cholephera kusambira mkuluyu adafera pomwepo koma anzake awiriwo anasambira mpaka kumtunda.
Zotsatira za kuchipatala cha boma la Nkhotakota zasonyeza kuti mkuluyu wafa kaamba kobanika.
Nkhalamo amachokera amachokera mmudzi mwa Ngaluka mdera la Sub T/A Nkhanga mboma la Nkotakota.
| 14 |
President Morales Wathawira Mdziko la Mexico Wolemba: Thokozani Chapola -content/uploads/2019/11/morales.jpg" alt="" width="265" height="355" />Wapita mdziko la Mexico-President Morales Patangodutsa tsiku limodzi mtsogoleri wa dziko la Bolivia Evo Morales atatula pansi udindo wake, wavomera kupita mdziko la Mexico ndi cholinga choti atetezedwe potsatira ziwonetsero zomwe zikuchitika mdzikolo.
Malipoti a wailesi ya BBC ati Pulezidenti Morales polankhula pa tsamba lake la twitter wati akumva kuwawa kuti akuchoka mdziko lake koma wanenetsa kuti abweleranso ndi mphamvu mdzikolo.
Padakali pano mkulu woona za chitetezo mdzikolo wauza asilikali a dzikolo kuti achite ubale ndi apolisi, omwe asemphana ndi otsatira chipani cha a Morales.
Anthu a mdziko la Bolivia akhala akuchita ziwonetsero zosonyeza kusakondwa ndi zotsatira za chisankho chomwe chinachitika mdzikolo mwezi watha pomwe Pulezidenti Morales anapambana kachinayi.
| 11 |
Amayi oyembekezera akulipira k10 000 Kusamvana kwabuka pachipatala cha chachingono cha Chikangawa mboma la Mzimba pamene amayi oyembekezera akulipiritsidwa K10 000 pokabereka. Amayiwo omwe auza Msangulutso ati ndi odabwa kuti mwana akangobadwa, achipatala akumalamula kholo lake kuti lilipire K10 000. Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Amayi oyembekezera akulipira K10 000 ku Chikangawa Kulibe komwe tingathawire, chipatala chathu ndi chimwechi, sitikudziwa ngati boma lakhazikitsa malamulo woti tiyambe kulipira mzipatala tikakabereka. Kudabwitsa kwake sakumatipatsa malisiti tikabereka, adatero mayi wina amene adakana kutchulidwa. Koma mkulu woona za umoyo mboma la Mzimba, Lumbani Munthali adavomera kuti amayi akumalipira koma izi zikuchitika kutsatira malamulo amene anthu ozungulira chipatalacho adagwirizana. Iye adati anthuwo adagwirizana kuti mayi aliyense amene sapita kuchidikiriro (kukadikirira pamene masiku ake obereka ayandikira) azipereka K10 000. Cholinga chathu ndichoti amayi azipita msanga kuchipatala osati kudikira matenda ayambe chifukwa ena amapezeka kuti aberekera panjira kapena kunyumba. Ndalamayo imagwira ntchito zosiyanasiyana pachipatalapo, adatero. Munthali adatsimikizanso kuti anthuwo sapatsidwa malisiti potsimikiza kuti apereka ndalamayo zomwe zingabweretse mavuto polondoloza ngati ndalamazo zikugwiradi ntchito yoyenera.
Ndalama iliyonse imafunika umboni monga lisiti kuti yalipilidwadi, apa tivomereze kuti zimalakwika ndipo ndawauza kuti athane ndi vutolo, adalongosola Munthali.
Iye adati amayi amene amalipira ndalamayo ndi amene apita mochedwa kuchidikiriro, amene aberekera mnjira kapena amene aberekera kunyumba. Amene amakadikirira kuchipatala salipira kanthu akabereka, adatero Munthali. Komabe ngakhale mfumu yaikulu Kampingo Sibande ikuti malamulowo akuwadziwa, iyo idati sikudziwa kalikonse ngati anthuwo akuyenera kulipira. Ife chindapusa chomwe tidavomereza ndi chokhudza kukwatiwitsa mwana osati izizi, adatero Sibande. Iye adati malamulowo pamene amakhazikitsidwa amafuna alimbikitse kuti amayi azipita kuchipatala pamene masiku awo ayandikira. Izi zikukhumudwitsa amayi oyembekezera. Malinga ndi mayi wina amene wangobereka kumene mwana wa mwamuna pachipatalapo, K10 000 ndi ndalama yambiri yomwe sangayipeze. Ngati adali malamulo, ndiye mwina bwezi atatidziwitsa kuti tiyambe kutsala ndondomeko yake. Apapa akutiranga koma osadziwa tchimo lathu. Komanso masiku anowa ndi munthu utiyo wa kumudzi angatulutse K10 000? adafunsa mayiyo. Mfumu James Lupeska ya mderalo idati ngati mayi salipira ndiye kuti pena amabwenzedwa ndikulemberedwa kalata yopita ku chipatala cha boma pa Mzimba kapena chipatala chachikulu cha Mzuzu Central.
| 6 |
Ambuye Stima Apempha Akhristu Athandize pa Maphunziro a Asemino Wolemba: Sylvester Kasitomu Mpingo wakatolika mu dayosizi ya Mangochi walimbikitsa akhristu ake kuti adzipereke pothandiza maphunziro osula achinyamata omwe akuchita maphunziro a unsembe.
Episikopi wa dayosiziyi ambuye Montfort Stima anena izi ku Mangochi Cathederal loweluka pa 24 August 2019 atangomaliza misa ya chaka chokondwelera nkhonse ya dayosizi-yo Augustuno Woyera.
Iwo ati asemino omwe ali mma seminale osiyanasiyana omwe akuchokera mu dayosizi-yo akusowa zambiri pa maphunziro awo kotero dayosizi-yo ikuyenera kufufuza ndalama zoposera 34 Million Kwacha, zothandizira asemino-wa pamaphunziro awo a pa chaka.
Kotero ambuye Stima alimbikitsa akhristu-wo kuti apitirize kudzipereka pothandiza kupititsa patsogolo ntchito za utumiki mu dayosizi-yo, monga momwe akuchitira padakalipano.
Asemino athu akufunika ndalama zambiri kuti apitilize maphunziro awo ndiye akhristu tigwirane manja pofuna kuthandiza ansembe amawa-wa, anatero ambuye Sitima.
Mwazina dayosizi ya mpingo wakatolika ya Mangochi ili ndi asemino omwe ali ku St. Peters komanso ku St. Anthony Kachebere Major Seminary okwana 32 ndipo nsemino aliyense amayenera kugwiritsa ntchito ndalama zosachepera 1 million pa chaka.
| 13 |
Papa Wakhazikitsa Thumba La Ndalama Zothandizira Mabanja Okhudzidwa ndi Coronavirus Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wakhazikitsa thumba la ndalama zothandiza mabanja omwe akuvutika kamba ka mliri wa Coronavirus.
Malinga ndi malipoti a Vatican Radio, Papa wakhazikitsa thumbali kuti lithandize mu dayosizi ya Rome mdziko la Italy.
Iye wati akudziwa kuti pali mabanja ndi anthu omwe ntchito zawo zatha kamba koti ntchito za chuma zalowa pansi mmalo ambiri ogwilira ntchito malinga ndi mliri wa Coronavirus.
Pambali pokhala mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse, Papa Francisco ndi episkopi wa dayozsizi ya Rome.
Kudzera mkalata yake ya pa 9 June 2020 yomwe likulu la Mpingo wa Katolika latulutsa zadziwika kuti Papa Francisco wakhazikitsa thumba la ndalama zothandiza mabanja ndi anthu mu dayosizi ya Rome omwe ntchito zawo zatha kaamba ka mliri wa Coronavirus.
Papa Francisco waika ndalama zokwana 1 million Euros zomwe ndi pafupi 850 million Kwacha ku thumbali lomwe akulitchula kuti Jesus the Divine Worker Fund.
Mkalata yofotokoza za thumbali iye wati akudziwa kuti pali mabanja komanso anthu omwe zithandizo zina nzina sizingawafikire ndipo ndi anthu amenewa omwe thumba lomwe wakhazikitsali liyese kuwafikira ndikupepusa mavuto awo pa nthawi imeneyi mpaka anthuwa adzafike poti zinthu zayamba kuwayendera.
Papa Francisco wapempha anthu ndi mabungwe akufuna kwabwino kuti athandize kuponya kangachepe ku thumbali. Ndipo mwapadera iye wapempha ansembe kuti akhale oyamba kuponya kangachepe ku thumbali.
Papa Francisco wathokoza kudzera mkalata yake ntchito zabwino zomwe zikuchitika mu Dioceseyi zothandiza anthu omwe akuvutika pa nthawi ya mliri wa Coronavirus.
Mmawu ake potsatira kukhazikitsidwa kwa thumbali, Cardinal Angelo de Donatis yemwe ndi Vicar General wa Diocese ya Rome wayamikira Papa Francisco chifukwa cha ganizoli ndipo wati ayetsetsa kuti cholinga cha Papayu chikwaniritsidwe.
Miyezi ingapo yapitayi Papa Francisco adakhazikitsa thumba la ndalama zothandiza anthu pa mliri wa Coronavirus mmaiko osiyana-siyana ndipo iye anali woyamba kuika ndalama za nkhaninkhani ku thumbali. Kuonjezera apo iye wakhala akupereka ku maiko osiyana-siyana thandizo la zipangizo za mchipatala pa nthawi iyi ya mliri wa Coronavirus.
| 6 |
Boma Lati Lithandiza Pokhazikitsa Malo Oyezera Coronavirus ku Chancellor College Boma lati ndilokonzeka kuthandiza sukulu ya ukachenjede ya Chancellor mu mzinda wa Zomba kuti ikhazikitse malo oyezera kachilombo ka Coronavirus.
Msaka: Tichitapo kanthu Nduna ya zamalamulo yemwenso ndi membala wa komiti yowona za nthenda ya COVID-19 mdziko muno, a Bright Msaka anena izi lachiwiri pambuyo poyendera ndikuona ntchito zomwe boma la Zomba likugwira polimbana ndi nthendayi.
Iwo ati ndi okhutira ndi malo oyezera omwe alipo padakali pano ku nthambi ya Biology ku sukuluyi omwe ati ali ndi zonse zowayenereza kupatulapo kusowa kwa zipangizo zoyezera nthendayi.
Taona kuti Chancellor College ili ndi zipangizo zoyenera kuyeza matenda a COVID-19 ndipo ikugwira ntchito zomwe achipatala angathe kugwira yomwe ndi mbali imodzi yomwe ife timakhazikitsira sukulu za ukachenjede kuti zizithandiza pamene pasowekera, anatero a Msaka.
Iwo ati boma ndilokonzeka kuthandiza aliyense yemwe waonetsa chidwi chothandiza nawo pa ntchito yolimbana ndi mliriwu.
| 6 |
Boma likonzekera el ninochilima Boma lati alimi ndi anthu mdziko muno asanjenjemere ndi lipoti la nthambi ya zanyengo loti chaka chino kukhoza kukhala mphepo ya El Nino ponena kuti zikachitika ilo ndi lokonzeka kuthana ndi mavuto amene angadze.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Saulos Chilima, adalengeza posachedwapa pamsonkhano wa atolankhani pofuna kupereka chilimbikitso kwa alimi ndi anthu onse.
Chilima:Boma litumiza alangizi ndi achitetezo mmadera osiyanasiyana Takhazikitsa thumba la ndalama zokwana K1 biliyoni zoti zitithandize kukonzekera mphepo imeneyi kuti isadzaononge, adatero Chilima.
Chilima adati ndalama zomwe boma lakhazikitsazi ntchito yake nkudzalimbana ndi mavuto monga kusefukira kwa madzi kapena ngamba zitati zachitika potsatira mphepo ya El Nino yomwe ikumvekayi.
Iye adati pokonzekera El Ninoyu, boma litumiza alangizi ndi achitetezo mmadera osiyanasiyana kuti mphepoyi itati yafika adzakhale athandizi a anthu populumutsa katundu ndi miyoyo ya anthu.
El Nino ndi mphepo yomwe imasokoneza ntchito za ulimi chifukwa chosapanganika. Nthawi zina mphepoyi imachititsa kuti mvula igwe yoononga pomwe nthawi zina imachititsa ngamba.
Mneneri wa unduna wa zamalimidwe Erica Maganga adati mvula ikagwa mopitirira muyeso, mbewu zimakokoloka pomwe kukachita ngamba mbewu zambiri zimalephera kucha.
Iye adati njira ziwirizi zimabweretsa vuto la njala ndi umphawi mdziko chifukwa anthu amakhala opanda chakudya ndi choti angagulitse kuti athandizike.
Chaka chatha mbewu zambiri zidakokoloka ndi madzi mvula itabwera moonjeza panthawi yochepa koma akatswiri adati izi sizidali zotsatira za mphepo ya El Nino koma kusintha kwa nyengo.
Mneneri wa nthambi yoona za nyengo, Sute Mwakasungula, wati anthu azitsatira zomwe nthambiyi ikunena pa mmene nyengo ikuyendera ndi kutsatira malangizo omwe nthambiyi ikupereka.
Iye adati mphekesera zina zomwe zimamveka pankhani yokhudza za nyengo zikhoza kusokoneza anthu, makamaka alimi omwe amakhala ndi nkhawa kuti mpamvu ndi zipangizo zawo zikhoza kupita pachabe.
Nthambi yathu ili ndi akatswiri omwe amadziwa momwe nyengo ikhalire ndipo amapereka malangizo a zomwe anthu angachite kuti asakhudzidwe kwambiri. Anthu azitsatira zimenezi, adatero Mwakasungula.
| 18 |
Munthu Woyamba Wafa ndi COVID 19 ku Botswana Dziko la Botswana lalengeza za munthu woyamba kufa kaamba ka nthenda ya COVID-19 mdzikolo.
Malipoti a wailesi ya BBC ati imfayi yadza patangodutsa maola ochepa dzikolo litalengeza za kupezeka kwa anthu atatu oyambilira kupezeka ndi kachilombo ka Coronavirus mdzikolo.
Wayimitsa zochitika zonse za mdziko la Botswana-President Masisi Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dzikolo, Slumber Tsogwane wati womwalirayu ndi mayi wina wachikulire wa zaka 79 yemwe anapita mdziko la South Africa ndipo atabwerako anayamba kumva kuzizira ndipo anamuika malo omupatula pa chipatala china komwe wafa patadutsa masiku anayi.
Tsogwane wati mayiyu anayikidwa mmanda ngati munthu wokaikiridwa kuti ali ndi nthenda yachilendo kaamba zotsatira zake zinali zisanatuluke ndipo zotsatirazi zatuluka atayikidwa kale mmanda pomwe zadziwika kuti wafa kaamba ka nthendayi.
Padakalipano mtsogoleri wa dzikolo Mokgweetsi Masisi walengeza kuti mdzikomo wagwa ngozi yaikulu ndipo walamula kuti zochitika zonse za mdzikolo ziyambe zayima kwa masiku 28.
Izi zikutanthauza kuti kuyambira lachinayi palibe amene akuyenera kuyenda kapena kugwira ntchito ndipo amene adziloredwa kuchoka mnyumba zawo ndi okhawo omwe akugwira ntchito zofunikira kwambiri mdzikolo.
| 6 |
Papa Wapempha Akhristu Akhale Odzichepetsa Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco, wapempha akhristu kuti akhale odzichepetsa ngati Yesu Khristu.
Papa Francisko Malinga ndi malipoti a wailesi ya Vatican, Papa Francisco anapempha akhristu omwe anasonkhana pa bwalo la St. Peters Square kuti akonde kupemphera pemphero la mthenga wa njelo kwa mai Maria, kuti ayesetse kuyenda mmapazi a Yesu Khristu.
Iye wati ndi zomvetsa chisoni kuti akhristu ambiri amalephera kutengera khalidwe la Ambuye Yesu Khristu chifukwa chokomedwa ndi zinthu za mdziko.
| 13 |
Papa Walimbikitsa Mtendere wa Mbanja Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse papa Francisco wati mtendere komanso umodzi ndi zofunika mbanja komanso mu mpingo.
Papa pa umodzi mwa maulendo ake oyendera anthu Papa Francisco walankhula izi lolemba pa Misa yomwe anatsogolera ku likulu la mpingo ku Vatican.
Iye wati akudziwa bwino kufunika kwa umodzi komanso mtendere mbanja maka pano pamene mabanja ambiri ali mnyumba zao pofuna kupewa nthenda ya COVID 19 yomwe yakhudza dziko lonse la pansi.
Papa Francisco watinso umodzi ndi mtendere ndi zofunika mu mpingo pofuna popewa maphokoso ndi kugawikana ndipo Iye wati ndi pemphero lake kuti umodzi ndi mtendere zipitirire mmabanja ndi mu mpingo momwe.
| 14 |
Boma la Zomba Lati Lakonzeka Kuthana ndi COVID -19 Ofesi ya zaumoyo mboma la Zomba yati bomalo lidayamba kale kukonza malo operekera chithandizo kwa anthu odwala nthenda ya COVID-19.
Mkulu wa za umoyo mbomalo Dr. Alexander Chijuwa wanena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi.
Iye wati ena mwa malowa ndi chipatala cha chikulu cha Zomba Central, chipatala cha Matawale, Pirimiti komanso Chancellor College ndipo kumeneko ndi komwe azisunga anthu omwe azipezeka ndi kachirombo ka Coronavirus.
Kukonzekera kunayambika pamene tinamva kuti mthendayi yafika mmaiko ena ndipo taonetsetsa kuti zipangizo zoyenera zafika kele mmalowa, anatero a Chijuwa.
Iwo ati akupitirizabe kupereka mauthenga kwa anthu ndipo ayeza anthu ochuluka ndipo padakali pano munthu mmodzi ndi yemwe wapezeka ndi nthendayi mboma la Zomba.
| 6 |
Fetereza wa makuponi akusowa, atero ena Pamene alimi ena ali kalikiliki kuthira fetereza wachiwiri mminda mwawo, Tamvani yapeza kuti fetereza wa makuponi akusowa mmidzi ina ndipo alimi ena sadagulebe.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Msabatayi alimi ena ochokera mmaboma a Dedza, Chitipa, Nkhotakota ndi Chiradzulu atsimikiza kuti fetereza adangofika kamodzi kokha ndipo atatha alimiwo adalonjezedwa kuti fetereza wina afika posakhalitsa koma ilo lidangokhala loto la chumba chifukwa kufikira pomwe timalemba nkhaniyi nkuti maso ali kunjira.
Koma mneneri wa unduna wa zamalimidwe, Sara Tione wati izi ndizabodza chifukwa fetereza wafikira madera onse.
Mwina ndifufuze kaye koma ndikudziwa kuti fetereza adafika madera onse ndipo alimi agula kale, adatero Tione.
Malinga ndi mkulu wa bungwe la mgwirizano wa alimi la Famers Union of Malawi (FUM), Felix Jumbe, ndondomeko zatsopano zikumalangiza alimi kuti azithira fetereza pomwe akubzala mbewu.
Fetereza wachiwiri athirenso pomwe chimanga chili ndi masamba asanu.
Malinga ndi Jumbe, alimi omwe achedwa kuthira fetereza wachiwiri akuthira pano. Iye akuti awa ndi mavuto aakulu kwa alimi.
Wilfred Ngonya wa mmudzi mwa Mkombanyama kwa T/A Mwaulambia mboma la Chitipa amalima chimanga ndi soya. Munda wa chimanga ndi wokula ndi yekala imodzi ndi theka. Ngati wathira fetereza amakolola matumba khumi. Kupanda fetereza akuti zimabweretsa mavuto kwa iye chifukwa matumba ngakhale anayi satuluka.
Iye adalandira kuponi koma fetereza ndiye vuto. Mmudzi mwawo akuti anthu 500 ndiwo adalandira makuponi koma omwe adagula sakuposa 200.
Makuponi tidalandira mu Novembala. Fetereza amabwera mu Disembala, atangotha ameneyo adati abwera wina koma mpaka lero tikungosunga makuponi.
Ndimathira fetereza wachiwiri chimanga chili ndi masamba awiri koma pano chimanga chili ndi masamba asanu. Boma litiganizire, aka ndikoyamba kuno kukumana ndi vutoli, adatero Ngonya.
Nako ku Dedza kwa T/A Tambala akuti mwa mafumu 42 sadalandire fetereza. Gulupu Lodzanyama ikuvomereza kuti zafika pa lekaleka.
Kumeneko fetereza akuti amafikira mma Admarc atatu: Mayani, Kafwafwa ndi Mphonde koma anthu ozungulira Mayani ndiwo adagula.
Zakumunda tsopano taiwala, tsiku lililonse tikumakaswera ku Admarc kuti timve zenizeni za fetereza koma palibe chikuchitika, adatero Lodzanyama.
Mkulu wina wa Admarc kumeneko yemwe tidalankhulana naye koma adakana kulemba udindo wake ndi dzina ponena kuti amawakaniza, adatsimikiza za nkhaniyo.
Mu Disembala tidalandira matumba 7 168, matumbawa amati afikire madera onse kuno koma adatha. Anthu osaposera theka ndiwo adagula. Adati tilandira fetereza wina tisadafike Januwale koma mpaka pano, adatero mkuluyo.
Nako ku Nkhotakota akuti zidachitikanso motero. Gulupu Mgomba ya kwa T/A Mangachanzi mbomalo yati fetereza adafika mu Disembala ndipo anthu ena sadagule.
Adati fetereza afika posakhalitsa koma kuli zii. Chimanga pano chili mmawondo chosathira fetereza. Ndakhala ndikupita kwa bwanamkubwa wathu koma chomwe amanena nkuti fetereza afika, adatero Mgomba.
Koma Jumbe wati boma lichite machawi pothandiza alimi chifukwa izi zisokoneza ulimi.
Alimiwa sikuti akunama, ngati boma likutsutsa izi lipite mmudzi mwa Chisaka T/A Mwadzama mbomalo komwe alimi sadagule fetereza. Ndidali komweko, alimi akudandaula, adatero Jumbe.
Iye adati alimi akangopeza feterezayo akuyenera asakanize wanthaka ndi wobereketsa chifukwa nthawi yatha kale.
Mndondomeko ya chaka chino ya zipangizo zotsika mtengo, boma lachipani cha PP kudzera mwa mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda lidaonjezera chiwerengero cha alimi omwe apindule ndi ndondomekoyi kuchoka pa 1.4 kufika pa 1.5.
| 4 |
Mwana wa zaka 13, mavuto osakata Ikakuona litsiro mvula siyikata. Mwambiwu wapherezera pa msungwana wina wa Sitandade 7 (yemwe sitimutchula dzina) pasukulu ina ku Chikwawa.
Izi zidadziwika achipatala atamupeza msungwanayo ndi chinzonono komanso mabomu potsatira kumuyeza mkulu wina atamugwirira kochapa. Mwanayo adapezekanso ndi kachirombo ka HIV. Pano anzake, ngakhalenso abale ake, akumusala, mpaka kukana kudya naye mbale imodzi; ngakhalenso kusewera naye chifukwa cha momwe mthupi mwake mulili.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mwanayo lero chidwi cha sukulu chikuzilala Pamapeto pake, aphunzitsi akuti chidwi cha mwanayo, yemwe ali ndi zaka 13, pamaphunziro chikulowa pansi, kupereka chiopsezo choti angalephere kukwaniritsa loto lake lodzakhala woimira ena pamilanduloya.
Mavuto a mwanayo adafika pena pa 21 January chaka chino, pomwe adapita kukachapa mmalo mopita madzi othirira madimba a nzimbe za kampani ya Illovo mbomalo. Apo nkuti mmudzi mwa mwanayo mulibe mjigo.
Kenaka, mwanayo akuti adangomva kuti tswereee! Bambo wina kutulukira mumzimbe tsidya linalo, nkudumphira mmadzimo ngati akungofuna kusambira. Koma adasambira mpaka kuoloka kufika tsidya lomwe kudali mwanayo.
Adandiopseza ndi mpeni.
Adati ndisakuwe chifukwa adati andipha. Kenaka, adavula malaya. Adanena kuti nanenso ndivule ndipo ndigone pansi, mwanayo adafotokoza, atazyolika.
Iye adaonjeza kuti bambo amene ndi wochokera mmudzi mwawo ndiye adamuchita chipongwecho. Ndinkamva kupweteka, koma ndinkangolira pansipansi chifukwa ndimaopa, mwanayo adafotokoza Lolemba lapitali pomwe mtolankhani wathu adalowera ku Chikwawa kuti akamve zovuta zimene zadza kaamba ka kusefukira kwa madzi.
Mwanayo, yemwe ndi nzime mbanja la ana atatu, adati bamboyo adatenga nthawi kuchita zachipongwezo, ndipo atamaliza adamuuza mwanayo kuti asakauze aliyense.
Kuchapa kudathera panjira. Iye adati atafika kunyumbako sadauze mayi ake zankhaniyo. Atapita kusukulu adakauza aphunzitsi ake amene adatengera nkhaniyo kwa makolo komanso kupolisi.
Apo mpamene bamboyo, Kennedy Chiseko wa zaka 36 yemwe amakhalanso mmudzi mwa mwanayo, adanjatidwa.
Ndipo nkhaniyi ndiyo mwanayo adakanena popereka umboni wake pamaso pa Gladstone Chirundu yemwe pa 11 March adagamula kuti Chiseko akasewenze zaka 8 kundende, atamupeza wolakwa pamlandu wogwirira mwana mosemphana ndi Gawo 138 la malamulo a dziko lino.
Komatu mwanayo akadamuyeza kaye ngati adapatsidwa kachirombo koyambitsa matenda a Edzi kuti achipatala amupatse mankhwala ochotsa HIV pasanathe maola 72 kuchokera pamene anagwiriridwa. Nchifukwa chiyani izi sizinachitike? Malinga ndi mneneri wapolisi ku Chikwawa, Foster Benjamin, padalibe danga loti nkutero, chifukwa nkhani ya mwanayo idafika kupolisi patadutsa maola 72.
Pokauza aphunzitsi ake kuti wachitidwa chipongwe nthawiyo idali itadutsa, adatero iye.
Malinga ndi aphunzitsi komanso bambo amwanayo, atamva za kugwiriridwa kwake adathamanga naye kuchipatala komwe zidasonyeza kuti adagwiriridwadi ndipo adawauza kuti apitenso. Atapitanso patatha milungu iwiri, achipatala adapeza kuti adali ndi matenda opatsirana pogonana a chinzonono ndi mabomu komanso kachirombio koyambitsa matenda a Edzi.
Malinga ndi lamulo limene Nyumba ya Malamulo idakhazikitsa chaka chatha, lokhudza matenda a Edzi, nkovuta kupereka umboni woti wakuti ndiye adapatsira wina kachirombo ka HIV choncho Aphungu adachotsa mfundo yonena kuti amene akukaikiridwa kuti adapatsa wina kachiromboka azizengedwa mlandu. Kuchoka pa nthawi yomwe mwanayo adauzidwa ndi a chipatala kuti ali ndi kachiromboka mpaka lero, moyo wake wakhala wodzadza ndi mavuto.
| 15 |
Apempha Achinyamata Asinkhesinkhe Mozama za Chiyitanidwe Chawo Achinyamata mdziko muno awapempha kuti adzipemphera komanso kusinkhasinkha mozama za chomwe iwo amafuna kudzakhala mmoyo.
Mwakhwawa: Achinyamata apemphere zolimba Mkulu wamu ofesi yowona ntchito za mabungwe a Papa la Pontifical Mission Societies (PMS), bambo Vincent Mwakhwawa anena izi lero pomwe mpingo wakatolika umachita chaka cha kuyitanidwa.
Iwo ati kupemphera komanso kusinkhasinkha mozama kungathandize achinyamatawa kuti avomere mayitanidwe awo mwanzeru.
Ansembe, asisteri kukondwelera tsikuli zaka zammbuyomu Tsiku limeneli mpingo unatipatsa achinyamata kuti apempherere ndipo asinkhe sinkhe zomwe akufuna azachite mtsogolomu chifukwa choti Mulungu ndi amene amatitsogolera nthawi zonse, anatero bambo Mwakhwawa.
Chaka chino zinthu zizinachitike monga nthawi zonse malinga ndi mmene dongosolo la tsikuli limayenera kukhalira kaamb ka mliri wa COVID-19.
| 13 |
Othawa madzi ati bola azibwerera kwao Mawu oti kwanu nkwanu mthengo mudalaka njoka lero akupherezeka pomwe anthu ena amene adathawa madzi osefukira kumunsi kwa chigwa cha Shire, maka ku Nsanje, akuti akufuna boma liwalole azibwerera kwawo ponena kuti ndi bwino akavutike kusowa pogona koma azikalima.
Nyakwawa Katandika ya kwa T/A Nyachikadza yomwe ikusungidwa pamsasa wa Bitilinyu mbomalo, yati iyo ndi anthu ake akuopa kuti ngati sabwerera msanga ndiye kuti sakhala ndi mwayi wolima, zomwe zingawabweretsere njala yoopsa chaka chino mpaka chamawa.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Anzathu chimanga chikupota, pamene ife sitidayambe ndi kulima komwe. Mvula sichedwa kusiya kuno. Ngati tingokhala mmisasamu, ndiye kuti tikuputa dala njala, Katandika adauzaTamvaniLachiwiri.
Koma mkulu woona zomangamanga kuofesi ya DC wa Nsanje, Kennedy Adamson, wanenetsa kuti ngati anthuwo akufuna kupita kapena akukakamirabe mmalo angoziwa ndiye sapeza nawo mwayi wa nyumba zotsika mtengo.
Boma limanga nyumba zotsika mtengo mmadera amene simukhudzidwa ndi ngozizi. Ndiye ngati ena akukana kusamukira kumtunda kapena akubwerera [mmalo momwe chaka ndi chaka mukhala vuto la kusefukira kwa madzi], sapindula nawo ndi ndondomekoyi, adatero Adamson.
Koma Humphrey Magalasi, amene akuyanganira msasa wa Bitilinyu, akuti ngakhale anthuwa akukakamira kubwerera, pali mantha kuti angakavutike chifukwa madzi sadaphwerebe.
Kodi akuti apita kuti? Kuli madzi okhaokhatu komwe amakhalako. Ngati panopa tidakasakabe kuti tipeze anthu amene tikuwaganizira kuti adapita ndi ndipo sadapezekebe, ndiye kuti zinthu zili bwino kumeneko?, adatero Magalasi.
Nawo azanyengo achenjeza kuti kugwa mvula yoopsa kuyambira Lachinayi lathali ndipo pali chiyembekezo kuti ku Chikwawa ndi ku Nsanje madzi asefukiranso.
Mneneri wa nthambi yoona zanyengo Elina Kululanga wati maboma a Blantyre, Zomba ndi Mulanje ndiwo ali pachiopsezo cholandira mvula yochuluka.
Ikhala yaziphaliwali komanso yamphepo ya mkuntho. Ndi mvula yambiri, chiyembekezo chilipo kuti kuchigwa cha Shire madzi asefukiranso, adatero Kululanga ouza Tamvani Lachiwiri.
Kodi nyakwawa Katandika akuti chiyani pa zomwe odziwa zanyengo akunenazi? Iyo ikufotokoza: Chadutsa chija ndi chinyama, sizingatheke kuti madzi otere adutsenso. Ineyo chibadwireni sikunadutseko madzi ngati amenewa. Tisaope, madzi amene aja apita. Malo olima alipo, tikalima kumtunda chifukwatu madziwa aphwerako kusiyana ndi momwe timachokako.
Kwa maola awiri amene Tamvani idakhala pamsasa wa Bitilinyu womwe ukusunga anthu oposa 3 000, nkhani yomwe anthu ambiri amakamba ndi yoti abwerere kwawo basi.
Ngakhale zakudya zikubwera pamsasawu, anthuwa akuti sakukondwa ndi momwe akuwagawira chakudyacho.
Tikuyenera tizidya katatu patsiku, koma tikumadya kawiri basi, komanso chakudya chake chochepa. Kodi ngati sitilima ndiye tizivutikabe chonchi? Boma litipatse mapepala apulasitiki kuti tikamangire nyumba ndipo litivomereze kubwerera kwathu, idatero mfumuyi yomwe idatinso mudzi wake wonse udathawa madzi oopsawo.
Izinso zili chonchi ndi kumsasa wa Makhanga ndi ku Osiyana mbomalo komwe, malinga ndi mkulu wa zaulimi Isaac Ali, anthu ena ayamba kale kutuluka mmisasa yawo.
Ndauzidwa kuti anthu ena akwezedwa mabwato ndipo abwerera. Akuti akukhala cha ku Khonjeni mbali ya Thyolo komwe kulibe chakudya. Kupitako nkovuta chifukwa cha mayendedwe, adatero Ali.
Mvula ya mphamvu idagwa kumayambiriro a mwezi uno ndipo maboma a Chikwawa, Nsanje, Phalombe, Zomba, Rumphi, Karonga, Thyolo, Machinga, Mangochi, Ntcheu, Chiradzulu, Mulanje, Balaka, Salima ndi Blantyre ndiwo adakhudzidwa.
Malinga ndi zomwe mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika walankhula Lachiwiri lapitali, anthu 174 000 atsamutsidwa mmalo mwawo kaamba koti nyumba zawo zakokoloka ndi madzi.
Iye adati sukulu 234 zagwetsedwa ndipo sukulu 181 ndizo zikugwiritsidwa ntchito ngati malo othawirako.
Mutharika adati chiyambireni mavutowa, boma lake lakhala kalikiriki kuthandiza anthu amene akhudzidwawa ndipo ndalama zoposa K38 biliyoni ndizo zikufunika kuti zithangate anthuwa.
| 5 |
Wodzaima pa mpando wa pulezidenti azapereka K2m Bungwe la Malawi Electoral Support Network (Mesn) ladzudzula bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) pokweza ndalama zomwe anthu ofuna kudzaima nawo pa zisankho zapatatu za chaka cha mawa azipereka.
Mkulu wa bungwe la MEC, Jane Ansah, Lachiwiri mu mzinda wa Lilongwe adalengeza kuti aliyense yemwe akufuna kudzaima nawo pa zisankho za mtsogoleri wa dziko lino akuyenera kudzapereka K2 miliyoni pamene abambo omwe adzapikitsane nawo pa mipando ya aphungu a Nyumba ya Malamulo adzapereka K500 000 ndipo amayi adzapereka K250 000.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Adzaimira MCP: Chakwera Ansah adalengezanso kuti abambo omwe akufuna kudzapikitsana nawo ngati makhansala akuyenera kudzapereka K40 000 pamene amayi adzapereka K20 000.
Koma mkulu wa bungwe la Mesn, Steve Duwa, wauza Tamvani kuti kusinthaku kubwezera mmbuyo anthu ena omwe akufuna kudzapikitsana nawo pa zisankhozo, koma mthumba mwawo ndi moperewera.
Duwa wati ndiwokhumudwa kuti sipadathe nthawi yayitali MEC chikwezereni ndalamazo.
MEC idakwezanso ndalamazo pa zisankho zapatatu za mu 2014 ndipo mabungwe osiyanasiyana omwe akulimbikitsa amayi kutenga nawo gawo pa ndale za dziko lino adadandaulanso kuti kusinthako kubwezera mmbuyo kampeni yawo.
MEC yapupuluma imayenera kudikira kuti papite zisankho zingapo isadakwezenso osati kumangokweza pa chisankho chilichonse chifukwa uku nkupweteka anthu omwe sangakwanitsa kupeza ndalama, adatero Duwa.
Adzaimira DPP: Mutharika Ngakhale malamulo oyendetsera zisankho amapereka mphamvu kwa bungwe la MEC kukweza ndalama zomwe anthu amapereka, koma Duwa adati mphamvuzo nzofunika kuzigwiritsa ntchito moyenera pokambirana ndi zipani za ndale kukwezako kusadachitike.
Koma Ansah adati akuluakulu a bungwelo adakambirana ndipo adaona kuti kukwezako nkoyenera.
Mkuluyu adati ndondomeko zina zonse zoyendetsera zisankho sizidasinthe.
Ansah adapempha zipani zandale kuti zitsatire ndondomeko zonse kaamba koti munthu akadzapezeka kuti ndiwosayenera adzamuthothola ndipo sipadzakhala mwayi woti chipani chake chidzapereke dzina la munthu wina.
Ansah adakumbutsanso zipani ndi onse omwe akufuna kudzaima nawo pa zisankho za chaka cha mawa kuti aliyense amene amagwira ntchito mboma ndipo akufuna kudzapikisana nawo pa zisankhozo akuyenera kutula kaye pansi udindo wake asadabwere poyera.
Padakali pano zipani zina za ndale zomwe zidaonetsa chidwi chofuna kudzapikisana nawo pa zisankhozo zidapangitsa kale misonkhano yawo yosankha atsogoleri moti panopa zikupangitsa mapulayimale wosankha anthu omwe adzaziimire pa mipando ya aphungu ndi makhansala.
Chipani cha Malawi Congress (MCP) chidasankha mtsogoleri wake Lazarus Chakwera kuti ndiye adzachiimire pa zisankho za chaka cha mawa pamene mtsogoleri wa Democratic Progressive (DPP) Peter Mutharika adzaimira chipanicho.
| 11 |
Yamikani Headmaster Fodya wa Bullets Dzina la Yamikani Fodya lawanda. Uyutu ndi mnyamata wokankha chikopa kutimu ya Flames komanso ku Big Bullets. Iyeyu wapatsidwa maina osiyanasiyana kaamba ka luso lake lomwe ochemerera mpira akuliyamikira monga mwa dzina lake. BOBBY KABANGO akumva za mbiri yake.
Fodya: Mulungu akakonza palibe angatsutse Tikambire za mbiri yako Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Ndimachokera ku Balaka. Ndine wa nambala 7 kubadwa mbanja la ana 8. Ndinenso wokwatira ndipo ndili ndi mwana mmodzi dzina lake Favour.
Ku Bullets udabwerako liti? Ndidafika mumzinda wa Blantyre mu 2009. Nthawiyo nkuti kutangoyambika chikho cha Presidential Cup ndiye anthu adaona luso langa mpaka kundiitanira kutimuyi.
Udalandiridwa bwanji? Kundirandira kudali bwino koma kupeza mwayi wosewera padavuta. Ndidapeza osewera ambiri, ngakhale ku training sindimapeza mwayi. Ngakhale kutulutsa timu yonseyo, mwayi wolowabe sumapezeka.
Nanga umasewera malo ati? Nthawiyo ndimasewera pakati, malo amene ndimasewera ku Young Soccer ya ku Dedza.
Zidatani kuti uyambe kusewera kumbuyo? Idangokhala pulani ya Mulungu chifukwa kochi wa timuyi panthawiyo, Meke Mwase, adandifunsa za malo amene ndimasewera ndiye ndidangoti kumbuyo. Basitu kuyamba kusewera kudali komweko.
Zidayamba kukuyendera mchaka chanji? Mu 2010. Chaka chimenechi ndidasankhidwanso wosewera amene wachita bwino kumbuyo. Koma kuchoka nthawiyo mpaka 2013 ndiye zidavuta chifukwa ndidavulala msana.
Wafala paliponse ndi luso lako, kodi ndi mankhwala? Mbale wanga, Mulungu akakonza palibe amene angatsutse. Pamene sizimayenda ndimalimbikirabe kuti tsiku lina zidzayende. Palibe mankhwala koma mphamvu yake basi. Si nzeru zanga koma chifundo chake cha Mulungu.
Malo amene ukusewera ku Flames umalimbirana ndi Francis Mlimbika, kodi simuchitirana nsanje? Francis ndi mbale wanga, ndimamupatsa ulemu ndipo ndimakondwera naye. Dziwani kuti nayenso Mulungu adamupatsa luso. Ngati lusolo lili la Mulungu, ine ndani kuti ndimuchitire nsanje? Kodi ukungotchula za Mulungu bwanji? Uli mpingo wanji? Mbale wanga, palibe munthu amene sadziwa kuti kumwamba kuli Mulungu. Ngakhale wakuba amadziwa. Tili mmasiku omaliza, palibe chomwe tingachite ngati iye palibe. Malembo amati ngati Iye samanga nyumba omangayo amanga pachabe. Nchifukwanso ndimatsogoza Mulungu pazonse. Ndikupemphera mpingo wa Seventh Day Adventist.
Ukutchulidwa maina osiyanasiyana, kodi mainawa adabwera bwanji? Tili ku Cosafa, onenerera mpira amanditchula kuti Soul Brother ati chifukwa cha tsitsi langali limafanana ndi oimba a gulu la Soul Brothers kumeneko. Kunoko anthu andipatsa dzina loti Headmaster chifukwa ndimapisira malaya 90 minitsi.
Kodi sumeta chifukwa chiyani? Nanga kupisiraku? Ndimasangalala ndi osewera mpira akale amene samameta wamba, mametedwe alerowa kudalibe. Komanso amapisira ngakhale ma jersey ndi makabudula awo adali aangono. Zimenezi zimandisangalatsa. Komanso ndimamukumbukira Chisomo Kamulanje amene adandiuza zambiri za malo amene ndimasewera aja. Pamene amachoka ku Bullets ndidanena kuti ndikufuna ndidzapange chinthu chomwe ndidzamukumbukire nacho.
| 16 |
Akhoti anyanyala ntchito Mavenda 40 omwe adamangidwa mu mzinda wa Lilongwe sabata yathayi ali mgulu la anthu zikwizikwi za anthu amene akhudzidwa ndi kunyanyala ntchito kwa anthu ogwira ntchito mmabwalo amilandu mdziko muno komwe kunayambika Lolemba lapitali.
Chifukwa chakusayenda kwa zinthu mmabwalo amilanduwa iwowa alephera kupeza belo kapena chithandizo china chilichonse ndipo afinyikabe mpaka kunyanyala ntchitoku kutatha.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Onyanyala ntchitowa ati akuchita izi pofuna kukakamiza boma kuti liyambe kupereka malipiro omwe adagwirizana mchaka cha 2006.
Apa akatswiri pa ndale, amabungwe komanso anthu otumikiridwa ndi mabwalowa ati boma likuyenera kulongosola izi madzi asadafike mkhosi.
Kuyambira Lolemba mabwalo amilandu adali otseka, ndipo pofika Lachitatu pomwe timasindikiza Tamvani, mabwalowo adali asadawatsegule.
Malinga ndi mkulu wa bungwe loona zaufulu wa anthu la Malawi Watch Billy Banda wati kunyanyala ntchitoko kwasonyeza kuti boma silikulabadira miyoyo ya anthu.
Banda wati ngati kunyanyalaku kungapitirire, Amalawi ambiri avutika chifukwa pali ena omwe sakuyenera kukhala kundende koma ali kumeneko chifukwa cha kunyanyala ntchitoku.
Mavenda 40 omwe adamangidwa ku Lilongwe pazipolowe amayenera kukaonekera kubwalo lamilandu Lolemba koma sizidatheke chifukwa cha sitalakayo.
Mneneri wa polisi mchigawo chapakati, John Namalenga, Lachiwiri adavomereza kuti anthuwa adalephera kukaonekera kubwalo lamilandu chifukwa choti kumabwaloko kudali kotseka.
Iye adati kunyanyalaku kukapitirira ndiye kuti zitokosi zamdziko muno zikhala zodzadza.
Ngati anthu achuluka mchitolokosi timakawasunga ku polisi za Kawale ndi Lingadzi. Koma ngati kunyanyalaku kungapitirire tisowa pogwira.
Kudzadzaku kungachitike ngati titamanga anthu ambiri pakamodzi chifukwa zimatheka kumanga anthu oposa 100 patsiku, adatero Namalenga.
Mphunzitsi wa zandale kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, Joseph Chunga, wati uku ndikupha ufulu wachibadwidwe makamaka kwa anthu omwe ali mmanja mwa apolisi chifukwa amayenera kukaonekera kubwalo lamilandu kuti akapatsidwe belo kapena kuti akadziwike ngati ndi wolakwa pa mlandu omwe amangidwira.
Monga mwa malamulo, pamayenera pasadutse maola 48 omangidwa asadakaonekere kubwalo lamilandu. Ngati izi sizidatsatidwe, ndiye kuti ufulu wako waphwanyidwa.
Iye adati kunyanyalako kukapitirira pali chiopsezo kuti boma lingatengerepo mwayi chifukwa lidziwa kuti munthu akamangidwa sakaonekera kubwalo la milandu.
Izi zikutanthauza kuti ulamuliro wotsatira malamulo watha, adatero Chunga.
Ndipo Osman Chimenya wa ku Kanjedza mumzinda wa Blantyre adavomerezana ndi Chunga ndipo adati boma likuyenera kukwaniritsa mgwirizano wake ndi ogwira ntchitowa.
Erick Gomani wa ku Malewule kwa T/A Kapeni mboma la Blantyre adaikira mangombe, ndi kuti anthuwa adalonjezedwa kuti apatsidwa malipiro atsopano kotero boma likuyenera kukwaniritsa.
Mneneri wa gulu lomwe likunyanyalali yemwenso ndi kalaliki wamkulu ku High Court mumzinda wa Blantyre, Austin Kamanga wati sasintha ganizo lonyanyala ntchito pokhapokha boma litayamba kupereka ndalama zomwe zidavomerezedwa ndi Nyumba ya Malamulo mchaka cha 2006.
Iye adati malipiro a anthu omwe amagwira ntchito zina kumabwalo amilandu amavomerezedwa ndi nduna ya zachuma zomwe akuti zidachitika mu 2006 koma boma silidafune kukwaniritsa.
Kuyambira 1997, malamulo akagwiridwe ka ntchito a ogwira ntchito kumabwalo amilandu amaunikidwa pakatha zaka zitatu, ndipo akaonedwa amatumizidwa kunyumba ya malamulo kuti aphungu akaunikire ndikuvomereza, adatero Kamanga.
Mu 2006, Nyumba ya Malamulo itavomereza komanso nduna ya zachuma itavomereza, anthuwa akuti sadalandire malipiro atsopanowo ndipo kukokanakokana kudayambika.
Kamanga adaonjeza kuti: Mchaka cha 2009, boma lidangolengeza kuti litionjezera malipiro ndi K15 pa K100 iliyonse koma sitikumvetsa kuti ndalama imeneyi imachokera pati? Tikufuna tiyambe kulandira ndalama zathu, apo ayi sitibwerera kuntchito, adalumbira Kamanga.
Nduna ya zachuma, Ken Lipenga, samayankha lamya yake ya mmanja pomwe Tamvani imafuna kulankhula naye.
Koma iye adauza atolankhani Lachiwiri msabatayi kuti unduna wake ukukambirana ndi okhudzidwa kuti ayankhe mavuto a anthuwa.
Iye adati alankhulapo pa nkhaniyo akangomaliza kukambirana ndi mbali zokhudzidwa pa nkhaniyo.
| 11 |
Wayilesi Ya Vatican Ikondwelera Zaka 70 Zowulutsa Maprogram Ku Africa Wayilesi ya likulu la mpingo wa katolika pa dziko lonse ya Vatican, chaka chino ichita chikondwerero chokumbukira kuti papita zaka 70 ikuwulutsa ma pologalamu ake ku Africa.
Malipoti akuti wayilesiyi inayamba kuwulutsa ma pologalamu ake ku Africa mchaka cha 1950.
Wayilesiyi ndi chida cha mphamvu chomwe likulu la mpingo wa katolika pa dziko lonse limagwiritsa ntchito pofalitsa mauthenga a Papa komanso nkhani zosiyanasiyana.
Papita zaka 89 kuchokera pomwe Vatican Radio yomwenso imadziwika kuti wayilesi ya Papa (the Popes Radio) idakhazikitsidwa mchaka cha 1931. Papa Pio wa 11 ndi yemwe adawulutsa mawu koyamba pa wayilesiyi. Uthenga wa Papa Pio wa 11 womwe udali mu chilatini udawuluka pa 12 February 1931.
Ngakhale kuti ma pologalamu a chingerezi adayamba kuwulutsidwa mchaka cha 1937, ma pologalamu a chingerezi opita kwa anthu a ku Africa adayamba mchaka cha 1950 zomwe zikutanthauza kuti chaka chino papita zaka 70 Vatican Radio ikuwulutsa ma pologalamu ake ku Africa.
Ma pologalamu oyambirira a chingerezi opita kwa anthu a ku Africa anali okhudza nkhani za likulu la Mpingowu, maphunzitso a Katikisimu wa Katolika, mbiri za anthu oyera ndi miyambi ya ku Africa.
Pambali pa mapologalamu owuluka pa wayilesiyi ena amawajambulanso pa ma cassette ndi ku watumiza ku Africa.
Zaka zikupita Vatican Radio inayamba kuwulutsanso mu ziyankhulo za ku Africa monga Kiswahili ndi Hausa.
Itachitika Sinodi ya ku Africa Vatican Radio inayamba kukonzanso ma pologalamu okhudza magawo osiyana-siyana a moyo wa anthu monga chilungamo ndi mtendere komanso ma pologalamu a chitukuko ku Africa.
Padakali pano ma pologalamu a Vatican Radio akuwulutsidwanso ndi ma wayilesi ambiri a chikatolika ku Africa monga Radio Maria.
Padakali pano wayilesiyi ikuwulutsa ma pologalamu ake mu ziyankhulo 47 ndipo ansembe a chipani cha ma Jesuit (Society of Jesus) ndi omwe amayendetsa wayilesiyi.
| 14 |
The Rain: Mnyamata wanthetemya Anthu ambiri otchuka makamaka amasewero, oyimba ndi azisudzo amakonda kudzitcha maina otchukira kusiya awo a pamchombo. Mchitidwewu sudayambire kuno ku Malawi, ayi, koma ngakhalenso kumaiko akunja ziliko. Tikakamba za kwathu kuno tili nawo maulendo a Soldier, Anonga, Piksy, Shakira, Safintra ndi ena. Omwe atchulidwa apawa ndi zitsanzo chabe koma alipo ambiri makamaka achinyamata omwe akutchuka ndi nyimbo zamakonowa. STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi Bright Vitsotso, mnyamata yemwe watchuka pawailesi ndi kanema ndi nyimbo zamakono ndipo iye akuti dzina lake lodyera ndi The Rain.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Vitsotso: Ndimagawa nthawi yanga Tandifotokozera kuti ndiwe ndani mnyamata.
Dzina langa ndi Bright Vitsotso wa kwa Waliranji mboma la Mchinji, koma ndikukhala ku Lilongwe.
Wati Bright Vitsotso, nanga The Rain akuchoka pati? The Rain ndi dzina lomwe ndimatchuka nalo pazoimbaimba. Pali maina awiri la The Rain ndi Young Star omwe anthu otsata nyimbo zanga amadziwa.
Umaimba chamba chanji? Ndimaphatikiza Rap ndi Hip Hop zomwe ndimaziimba motsatira mingoli ya Chifirika. Panopa ndidapanga chikole ndi kampani yojambula nyimbo ya Dash Travellers Entertainment ndipo ndikugwira nawo bwino kwambiri ntchitoyi.
Luso lako lidayamba liti? Chilakolako choimba chidandiyamba mchaka cha 2005 pomwe ndinkaimba ndi anzanga koma zidali ngati zamasewera chabe. Ndikukula ndidayamba kulemba nyimbo zokhudza zinthu zochitikadi mmoyo wa munthu nkumayeserera kuziimba uku ndikudzijambula ndekha nkuona kuti zikumveka bwino ndithu.
Pakalipano uli ndi nyimbo zingati? Ndili ndi nyimbo zingapo, yoyamba kujambula idali Chikumbuntima yomwendidathandizana ndi Peter Banda ndi Mabilinganya Empire. Kenako ndidajambula Swazi ndi Mabilinganya Empire kenako Honey yomwe ndidajambula ndi Katelele Chingoma. Nditangomaliza imeneyi ndidajambula Ndikuopa ndi Lady Pace nkupuma kaye.
Nyimbo zako zimakhala ndi uthenga wanji? Nyimbo zanga zimakamba za mmene moyo ulili ndi nkhani zochitikadi. Sindifuna kuimba nyimbo zokhala ngati nthano, ayi, koma zoti munthu akamamvera azitha kulumikiza zomwe ndikunena ndi zomwe amakuna nazo kapena kuona mmoyo.
Kupatula zoimba, china chomwe umachita ndi chiyani? Kupatula kuimba ndimalembanso mafilimu, kuvina, kusewera mpira komanso ndidapanga za magetsi ku Yunivesite ya Nairobi ku Kenya kenako ndidagwirapo ntchito mmapolojekiti a Airtel kwa zaka 5 koma pano ndikupitiriza maphunziro ku United Arab Emirates.
| 9 |
WESM Ikuthandiza Alimi Kupanga Manyowa Bungwe la Wildlife and Environmental Society of Malawi (WESM) lati ndilokhutira ndi mmene alimi a mdera la Chingale akuchitira pa maphunziro omwe akuwapatsa.
Mmodzi mwa akuluakulu a bungweli a San Daniel Nkunga ndi omwe anena izi ku Chipini mboma la Zomba pomwe amayendera alimi ndi kuona ngati akutsatira bwino njira za ulimi zomwe alimiwa adaphunzira.
Bungwe la WESM likuphunzitsa alimi a mderali kapangidwe ka manyowa, pogwiritsa ntchito zinthu zosavuta kupeza mmadera mwawo.
Akutsatira zomwe tikuwaphunzitsa chatsala ndi choti akazichite kumunda kwawo. Alimi kuno amadandaula ndi kukwera mtengo kwa feteleza ndi chifukwa chake tinawaphunzitsa kapangidwe ka manyowa pogwiritsa ntchito zinthu zopezekeratu, anatero a Nkunga.
Mmodzi mwa anthu omwe anachita nawo maphunzirowa a Hanne Lihonga ayamikira maphunzirowa ponena kuti athandiza kuchulukitsa zokolora zawo cha chino.
| 4 |
WLA Yalowelerapo pa Nkhani za Nkhanza Bungwe la Women Lawyers Association mogwirizana ndi bungwe la Chanco Gender Justice Clinic lolemba layamba ntchito yodziwitsa anthu a mu mzinda wa Zomba, malamulo okhudza nkhani za nkhanza za mbanja.
Poyankhula pa zochitikazo mmodzi mwa akuluakulu a bungwe la Women Lawyers Association, Professor Ngeyi Kanyongolo wati cholinga cha zochitakazi ndi kuthandiza anthu amene ali ndi nkhawa pa nkhani za malamulo okhudza nkhanza za mbanja.
Professor Kanyongolo yemwenso ndi mphunzitsi wa za malamulo ku Chancellor College wati nthawi ino pomwe dziko la Malawi likukamba nkhani ya masiku 16 othetsa nkhanza za pakati pa amayi ndi abambo, magulu awiriwa abwera pamodzi pofuna kuti athandidze anthu kuti amvetse momwe nkhani za malamulo zimayendera.
Tili ndi Street Law Clinic yomwe cholinga chake ndi kuthandiza anthu amene akukumana ndi nkhanza komanso kuwadziwitsa kuti malamulo pa nkhani zimenezi amati bwanji, anatero a Kanyongolo.
Polankhulanso President wa Chancellor College Gender Justice Clinic ku nthambi ya za malamulo, Kilayibi Chinsinsi Kasinja wati akufunitsitsa kupereka uphungu wa zamalulo kwa anthu pofuna kuthetsa nkhanza zomwe amayi amakumana nazo.
Tikufuna tikumbukire nawo masiku amenewa ndipo ndi pofunika kuchitapo kanthu pothetsa nkhanza. Ife ma Lawyer timadziwa za malamulo koma anthu wamba samadziwa zimenezi, anatero a Kasinja.
| 14 |
Makuponi si yankho, ingosiyani Ngakhale boma lili kalikiliki ndi ndondomeko ya zipangizo zotsika mtengo, mphunzitsi wa zandale Joseph Chunga komanso mkulu woona zaufulu wachibadwidwe Billy Banda ati ndi bwino boma lithetse ndondomekoyi chifukwa kayendetsedwe kake kakusempha ovutika komanso sikakutukula anthu.
Koma boma lamenyetsa nkhwangwa pamwala ponena kuti lilibe maganizo othetsa ndondomekoyi padakalipano chifukwa ndi ndondomeko yokhayo imene ingathetse njala ndi umphawi mdziko muno.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mwachitsanzo, mndondomeko ya chaka chino, ovutika 44 000 achotsedwa pamndandanda wolandira nawo zipangizo zotsika mtengo chikhalirecho mbajeti ya chaka chino, K60.1 biliyoni ndiyo yalowa kundondomekoyi.
Chaka chatha K40.6 biliyoni ndiyo idalowa kundondomekoyi yomwe idapindulira ovutika 1 544 000 zomwe malinga ndi Banda akuti nkutheka ndalamazi zikulowa penapake.
Ndondomeko ya zipangizo zotsika mtengo ndi yofunika kulikonse ndipo nanenso ndimavomereza, koma mmene zikukhalira ndi bwinonso ndondomekoyi ithe, watero Chunga.
Chunga wati kafukufuku yemwe adapanga adapeza kuti ndondomekoyi ikupereka mafunso ambiri ngatidi dziko lino liyenera kupitiriza ndondomekoyi.
Funso ndi loti kodi dziko lino likuyenera kupitiriza ndondomekoyi mpaka liti? Komanso kodi kufunika kwake nkotani? Ena akuti ovutika akuyenera akhale ndi ndondomekoyi koma nanga ovutikawo akuthandizidwadi? Nanga ovutikawo akhale ati? Chifukwa ena akumalemba abale awo kapena akudziwana ndi mfumu, zomwe zikusemphana ndi zomwe tikufuna, adatero Chunga.
Lipoti lomwe boma mmwezi wa March chaka chino lidatulutsa pounguza mmene ndondomeko ya 2012/2013 idayendera, likuti fetereza wa K120 miliyoni sadapindulire ovutika.
Lipotilo, lomwe lidatsimikizidwa ndi Tione, lidati ndalamazo zidali za matumba 9 100 a fetereza. Feterezayo akuti wambiri adasempha ovutika ndi kukapindulira anamadyabwino.
Mndondomeko yathayi alimi ambiri adalandira mchenga mmalo mwa fetereza, zomwe sizidadziwike phata lake.
Chunga akuganiza kuti mwina ndalama zomwe zalowa mndondomekoyi atazigulira chimanga chogawira ovutika zingapindule.
Tikukamba za K60.1 biliyoni, ndalamayi ndi yambiri, pena tikuganiza kuti bwanji atakagula chimanga kumaiko akunja ndi kudzagawa kwa anthu ovutikawo, sizingathetse mavutowa? adatero Chunga.
Koma mneneri muunduna wa zaulimi Sara Tione wati ndi bwino kuphunzitsa munthu kuwedza nsomba mmalo momugawira chifukwa tsiku lililonse azigogoda pakhomo pako kuti umugawire.
Ndondomekoyi ikuphunzitsa anthu kawedzedwe ka nsomba kuti mawa akawedze okha osati kuwaphunzitsa kupempha. Inde ndondomekoyi ikukumana ndi zokhoma, komabe tikuyesetsa kuti zilongosoke.
Ndiponso tiyitanitsa bwanji chimanga kuchokera kunja pamene nthaka ndi zina zotero tili nazo mdziko muno? adatero Tione.
Pa za kutsika kwa anthu amene alandire zipangizozi, Tione wati izi zachitika chifukwa anthu 44 000 adangowonjezeredwa chaka chatha komanso wati kukwera mtengo kwa fetereza ndiko kwachititsa zimenezi malinga ndi nkhani ya zachuma mmene ikuyendera mdziko muno.
Tione wati posakhalitsapa zipangizozi ziyamba kufika mmadera ena mvula yoyamba isanagwe.
Koma Banda akuganiza kuti boma lachulutsa dala ndalama zopita kundondomekoyi pofuna kuyambitsa ndondomeko zina.
Dziwani kuti ndalamayi yachuluka kwambiri komanso chiwerengero cha opindula chachepa. Izi zimanditanthauzira kuti mwina boma likufuna ligwiritse ntchito ndalama yochepa kundondomeko ya zipangizo zotsika mtengo pamene zina zikulowa mmapolojekiti ena amene ife sitingawadziwe.
Iye akuganiza kuti K60.1 biliyoni ikungolemeretsa ena osati ithandiza ovutika. Banda akuti ndi bwono boma lithetse ndondomekoyi ndi kuyamba ina yomwe ingapindulire Amalawi onse.
Mneneri wa chipani cha DPP Nicholas Dousi wati akadzalowanso mboma adzapitiriza ndondomeko yopereka zipangizo zotsika mtengo kwa alimi koma adzayesetsa kuti ziphuphu zithe.
Koma tidalephera kumva maganizo a zipani zina monga MCP ndi UDF pankhaniyi kaamba koti titawayimbira mafoni awo ankangoitana koma samayankha.
Koma mtsogoleri wakale wa chipani cha MCP John Tembo, yemwenso ndi mtsogoleri wa zipani zotsutsa boma mNyumba ya Malamulo, adati akadakhala kuti ali mboma bwenzi atayambitsa ndondomeko yoti fetereza wotsika mtengo afikire aliyense, osati osaukitsitsa okha ayi.
| 10 |
Mafumu atekeseka ndi bilu ya malo Akufuna akhalebe ndi mphamvu pankhani yogawa kapena kugulitsa malo: Mafumu Mafumu ena mdziko muno aopseza kuti achita zionetsero ngati lamulo lokhudza malo lingasinthe kuti iwo asakhalenso ndi mphamvu pogawa malo.
Mawu a mafumuwa akudza pamene mabungwe a Landnet, Farmers Union of Malawi (FUM) ndi Womens Legal Resource Centre (Wolrec) ali yakaliyakali kumva maganizo a anthu pa Bilu yokhudza malo (Customary Land Bill).
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Pali maganizo oti lamuloli lisinthe kuti mafumu asamakhale ndi mphamvu zonse pamalo ndipo mmalo mwake pakhale komiti yomwe iziona za malo komanso kuti pakhale anthu othandizira nkhani za malo osati nduna za mafumu monga zilili panopa.
Mafumu akwiya ndi ganizoli ndipo anenetsa kuti zikasinthadi iwo achita zionetsero kusonyeza mkwiyo wawo ngati eni malo.
Tikati gogochalo timakamba malo. Ufumu ndi malo; popanda malo palibe ufumu; komanso popanda ufumu palibe malo. Ngati wina akufuna kukhudza malo ndiye akukhudzanso mafumu. Akachotsa malo kuti asakhalenso mmanja mwathu ndiye kuti achotsa ufumu wathu, T/A Kabunduli wa mboma la Nkhata Bay adauza Tamvani mosapsatira mawu.
Apa sitikuopanso, Pulezidenti ndi aphungu komanso anthu adziwe kuti pavuta ngati akufuna akhudze malo, adapitiriza.
Malipoti akhala akumveka kuti mafumu ena akugulitsa malo mwachinyengo komanso mosafunsa eni malowo omwe ndi mafumu angonoangono.
Koma Kabunduli akuti pasakhale mantha amenewo chifukwa mafumu amene akukhudzidwa ndi ziphuphuwa si mafumu.
Si mafumu amenewo, komanso lamulo lisasinthe chifukwa zotere zachitika. Sitikusintha ganizo lathu, lamulo lisasinthe chifukwa kuli ngati kuchotsa ufumu wathu, adanenetsa Kabunduli.
Nkhani zokhudza malo sizikukata. Ku Ntcheu mkangano wa malo uli mkati pamene makampani a Crown Plantation Limited ndi Mota Engil atengera nkhani ya malo kubwalo la milandu.
Makampaniwa akuganizira T/A Masasa kuti adagulitsa malo amodzimodziwo kwa makampani awiriwo.
Ngati lamuloli lisinthe ndiye kuti komiti yomwe ikubwera ndiyo izidzakhudzidwa ndi kagulitsidwe ka malo ndipo pakadzakhala kusamvana, anthu ena apadera ndiwo azidzayendetsa nkhaniyo, osati mafumu kapena nduna za mafumu monga zilili panopa.
T/A Kaphuka wa mboma la Dedza limodzi ndi Senior Chief Kachindamoto komanso T/A Nyambi wa mboma la Machinga, akulankhula Chichewa chofanana kuti iwo sangatchedwenso gogochalo ngati mphamvu zawo pa malo zachotsedwa.
Gogochalo ndi mwini nthaka, ndiye akufuna awachotsenso panthakapo? Lamulo lisasinthe. Nanga anthu amene adapempha malo kwa gogochalo awatani? Tipemphe amene akufunsa maganizo a anthuwo kuti aitanitse msonkhano wa mafumu kuti tikamve bwinobwino chomwe akufuna, adatero Kaphuka, yemwe adati sadakumanepo ndi amabungwewa.
Atha kusintha mbali zina za lamuloli koma pokhapo poti mafumu asamakhale ndi mphamvu pamalo ndiye izi sizotheka, ayi. Tikufuna tisachotsedwe mphamvu zathu pamalo, adatero Nyambi.
Koma Emmanuel Mlaka, yemwe akuyendetsa ntchitoyi kubungwe la Landnet wati ntchito ili mkati ndipo pafupifupi mafumu 8 pa 10 alionse akukana kuti lamuloli lisinthe.
Takhala pachigawo cha pakati kwa sabata zitatu kulankhula ndi mafumu, sabata ikubwerayi tikulowera ku Karonga. Pazomwe tapeza, mafumu akukana kuti lamuloli lisinthe pamene anthu wamba akuvomera kuti kusintha kukhalepo.
Chomwe mafumu akukanitsitsa nkuti pakhale komiti yomwe iziyendetsa za malo komanso kuti pakhale anthu amene aziwathandiza kuzenga nkhani za malo. Akunena kuti ali ndi nduna zawo zomwe zimawathandiza kotero palibenso kufunikira koti pakhale anthu ena apadera, adatero Mlaka.
Gift Mauluka wa bungwe la Worlec akuti ntchitoyi ikupita kumapeto.
Sabata yathayi Mauluka adali mboma la Thyolo kwa Mfumu Khwethemule komwe mafumu adatemetsa nkhwangwa pamwala kuti lamuloli lisasinthe.
Mafumu akukana koma anthu akuvomereza kuti kusintha kukhalepo. Ife tilemba zomwe anthu akunenazo ndi kutumiza, adatero Mauluka.
Pa 2 June 2013, aphungu a Nyumba ya Malamulo adadutsitsa gawo lina lokhudza Biluyi yomwe Pulezidenti Joyce Banda adakana kusayinira ponena kuti iwunguzidwenso.
Bungwe la Alliance for Green Revolution in Africa (Agra) ndilo likupereka thandizo kuti mabungwewa agwire ntchito yofunsa anthu pa za lamuloli.
| 8 |
Bwanamkubwa Achenjeza za Ngozi Zogwa Mwadzidzidzi Wolemba: Thokozani Chapola Bwanankubwa wa boma la Zomba Dr. Raphael Piringu wachenjeza anthu a mbomalo kuti akonzekere ngozi zokugwa mwadzidzidzi pa nthawi ino pomwe mvula yatsala pangono kugwa.
Ngozi ngati izi akuti zitha kuchitikanso chaka chino Dr. Raphael Piringu amayankhula izi lero mbomali pa nsonkhano wa atolankhani ndipo wauza atolankhaniwa kuti ali udindo waukulu wodziwitsa anthu zangozi zogwa mwadzidzidzi zomwe zingabwere mu nyengo ino ya mvula.
Dr. Piringu ati kaamba ka nyengo yotenntha imene ilipo padakali pano, kumayambiliro a nyengo ya mvula kukhala mphepo ya mkuntho yomwe iwononge nyumba komanso zinthu zina.
| 18 |
Boma Lapempha Mabungwe Athandize Zipatala Zakumidzi Boma lapempha mabungwe mdziko muno kuti athandize zipatala zingono-zingono ndi zipangizo zozitetezera ku kachirombo ka Coronavirus kuti anthu adzitha kuthandizidwa kuchokera madera akumidzi komweko.
Wachiwiri kwa nduna yowona za kusasiyana pakati pa amayi ndi abambo, ana komanso chisamaliro cha anthu, Grace Kwelepeta wanena izi ku chipatala chachingono cha Domasi mdera la Zomba Malosa, pomwe kampani ya Amezam Shipping Company limapereka zipangizo zosiyanasiyana zozitetedzera ku kachilombo ka Coronavirus.
Iye wati zipatala za mtauni zimalandira matenda ochokera mzipatala za mmadera a kumudzi choncho ndi kofunika kumathandiza zipatala zakumidzizi ndi zipangizo zokwanira.
Kwambiri zipatala zantauni zimalandira matenda kuchokera mmidzi ndipo tikuyenera kusamala zipatala zakuno kumidzi ndicholinga kuti zipatala zantauni zisadzadze, anatero a Kwelepeta.
Mmawu ake mmodzi mwa akulu akulu a kampani ya Amezam Shipping kuno ku Malawi a Benson Mtonga apempha akuluakulu a malonda kuti nawonso athe kuthandiza zipatala za madera akumidzi ndi katundu wodzitetedzera ku kachirombo ka Coronavirus.
Pempho langa ndi lakuti amabizinesi athandize potengera zomwe bungweli lachita pothandiza ndi zochepa zomwe amapeza, anatero a Mtonga.
| 6 |
Lipy G: Woimba za chinyamata Masiku ano kwadza oimba achinyamata amene akumaimba nyimbo zawo zothamanga kwambiri. Kulitu anyamata monga Nepman, Blasto, Piksy ndi ena otero amene lusoli lakhazikika. Komansotu kuli anyamata ena amene akuonetsa kuti ataikapo mtima akhoza kusadabuza izi. Awa ndi monga Lipy G, amene adacheza ndi CHIMWEMWE SEFASI motere: Ndikudziwe Dzina langa lenileni ndi Edward Fortiner, ndine wachiwiri kubadwa mbanja la ana 6. Ndimachokera chigawo chakumwera mboma la Nsanje.
Chisale watuluka nkumangidwanso Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Lipy G: Ena amatipondeleza Kodi kuimba zadansi udayamba liti? Kuimba ndidayamba pakale ndithu, nthawi imeneyo ndili kusukulu ya sekondale, ndi pamene ndimazindikira kuti ndili ndi luso losangalatsa anthu kupyolera mmaimbidwe , munyimbo za dansi.
Kodi ndi chani chomwe unapindulako kuchoka maimbidwe? Ine kudzera mmaimbidwe malinga ndi ndalama zomwe ndimapeza kuchoka ku zoimbaimba zandithandiza kwambiri moti pano ndinatsegula malo wojambulira nyimbo amene amatchuka ndi dzina loti Future Records. Uku ndi ku Zingwangwa mumzinda wa Blanytre.
Kupatula kuimba umachitanso chiyani pamoyo wako wa tsiku ndi tsiku? Inetu ndimapanga bizinesi komanso ndine katswiri pankhani yojambula nyimbo.
Kodi chimbale chako chatsopano chituluka liti? Mutu wake ndi chani? Chimbale changa chikuyembezereka kutuka mapeto a mwezi wa October, chomwe chikhale ndi nyimbo zokwana khumi zomwe zayimbidwa mu chiyakhulo cha Chichewa ndi muchizungu. Ndipo kuyambira pa 15 October 2015 mpomwe ndiwadziwitse Amalawi zambiri.
Kodi ndi mavuto ati omwe oimba zadansinu mumakumana nawo? Mavuto omwe timakumana nawo ndi monga kupita kuzoimbaimba koma osapatsidwa ndalama yomwe tidagwirizana, kumeneku ife timaona ngati tikuponderezedwa komanso anthu ena kuti atukule luso lathu amafuna kuti tiwapatse ndalama.
Kodi ndi anthu ati omwe unaimbako nawo nyimbo limodzi chiyambireni kuimba pa Malawi pano? Inetu chiyambireni kuimba pa Malawi pano ndiyimbako nyimbo ndi anthu ambiri monga Blasto, Nepman. Awa ndi akadaulo komanso ndaimbako maiko akunja monga Botswana, south Africa ndi Uganda.
Pomaliza tandiuze zomwe umakonda.
| 9 |
Papa Wapempha Athu Kuti Azisamalira Achikulire Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wati anthu achikulire akuyenera kusamalidwa bwino.
Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican, Papa walankhula izi mu uthenga wake wa pa lamya wopita ku parishi ya Paulo Woyera wa Mtanda mu Diocese ya Rome.
Iye wati anthu achikulire akufunika chisamaliro chokwanira komanso kuti akufunika kukhala nao pafupi ndi kumacheza nao.
Bambo Roberto Cassano yemwe ndi bambo mfumu wa parish ya Paulo Woyera Wa Mtanda (Saint Paul of the Cross) mu Diocese ya Rome wati anali wodabwa msabata yangotha kumeneyi pomwe analandira lamya ndipo atamvetsera bwino mau a munthu yemwe amalankhula naye anazindikira kuti anali kulankhula ndi Papa Francisco.
Papa Francisco monga episkopi wa diocese ya Rome adayendera parishyi pa 12 April mchaka cha 2018.
Ndipo umodzi mwa ma utumiki opezeka mparishiyi, womwe Papa Francisco adachita nao chidwi ndiwo wosamalira anthu achikulire.
Kudzera pa lamyayo Papayu walimbikitsa bambo Cassano kuti apitirize ntchito yotamandika yosamalira anthu achikulire omwe kawiri-kawiri amaiwalidwa.
Mmawu ake bambo Cassano wati ndi zopatsa chidwi kulandira lamya ya chilimbikitso kuchokera kwa Papa Francisco yemwe akukumbukirabe za ulendo wake wokacheza mparishiyi.
Bambo Cassano wati wachita chidwi kuti kangapo konse pa lamyayo Papa Francisco anapempha parishyi kuti izimupemphelera.
Iye watinso lamya ya Papa Francisco yawalimbikitsa kwambiri ngati parish pa utumiki wao wosamalira anthu ovutika mu njira zosiyana-siyana makamaka anthu achikulire.
Mmaiko ambiri pa dziko la pansi kuphatikizapo dziko la Malawi anthu achikulire akukumana ndi mavuto osiyana-siyana. Mwa zina zomvetsa chisoni nkuti anthu achikulire ku Malawi amagniziridwa kuti ndi afiti komanso omanga mvula.
| 14 |
Eid al Adha: Chikondwerero chopereka nsembe Chaka ndi chaka a chipembedzo cha Chisilamu amakhala akuzinga ziweto nthawi ina. Pa mwambowu, Asilamu amakhala akutsatira zomwe Mulungu adalamula Abraham zaka zammbuyo. STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi Sheikh Malekano Rajab ndipo adakambirana motere: Poyamba, ndikudziweni.
Chisale watuluka nkumangidwanso Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Ndine Sheikh Malekano Rajab ndimatumikila pamzikiti wa pamsika wa Area 22 ku Lilongwe.
Kodi chaka ndi chaka Asilamu amakhala ndi mwambo wopha ziweto talongosolani kuti zimakhala bwanji? Mwambo umene uja timakhala tikukumbukira zomwe Mulungu adauza Abrahamu kalelo nthawi yomwe adavomera kupereka mwana wake Ishmael nsembe. Akuti azipereka mwanayo nsembe, Mulungu adatumiza nkhosa ndipo mwanayo adapulumuka. Mulungu adalamula Abrahamu kuti chaka chilichonse Asilamu azikhala ndi mwambo umenewu ngati chikumbutso komanso kulemekeza Mulungu.
Mwambowu umachitika liti? Umachitika tsiku la khumi (10) la mwezi wa chisanu ndi chinayi mkalendala ya Chisilamu. Pakafika pa 1 mwezi umenewo msilamu aliyense amayenera kuyamba kusala kwa masiku 10 ndipo kusalako kumatha tsiku la nambala 10 lomwe kumakhala kuzinga ziweto kapena chikwenderero cha Eid al Adha. Chimachitika nchiyani pa tsikuli? Msilamu amayenera kugula chiweto monga ngombe kapena mbuzi nkupha. Nyama yake nkugawa koma naye mwini wake amayenera kutengapo gawo osangogawa yonse ayi. Kupha nyamako kumatchedwanso Qrubani.
Chiweto chake chimayenera kukhala chotani? Chiweto chikhoza kukhala chilichonse koma chikhale chopanda chilema kapena choti chidakokako ngolo kapena chidalimako. Chikhale chiweto chalunga ndipo chopanda ngakhale chilonda pathupi lake komanso chathanzi.
China chimachitika nchiyani? Lisadafike tsikulo, Asilamu a ndalama zawo amapita ku Mecca. Ulendo wopita ku Mecca umatchedwanso kuti haji ndipo ndi imodzi mwa nsanamira za Chisilamu. Omwe alibe ndalama amakhala kumudzi koma nawonso amakhala akutsatira zoyenera kuchita kuti tsikulo lisadetsedwe.
Nanga wina akaphonyetsa monga kupha chiweto chodwala zimakhala bwanji? Pamenepo nsembe imeneyotu siyilandiridwa chifukwa ndiyodetsedwa ndipo ndiyosayenera kuperekedwa kwa Mulungu. Nthawi zonse munthu amayenera kukumbuka kuti iyi ndi nyengo yoyera yoyenera kuyeretsedwa.
Nanga aja amakhala akuimbawa amatinji? Amene aja sakhala akuimba nyimbo, amakhala akupemphera pemphero lomwe mngelo Gabriel ankanena akudzapereka nkhosa yomwe Abrahamu adasinthitsa ndi mwana wake yemwe adakonzeka kukamupereka nsembe. Pemphero lake limati Mulungu ndi wamkulu palibe ofanana naye ndipo iye ndiye tate basi.
Nanga ochepekedwa ndalama sizingatheke kugula nyama yophaipha nkugawa? Ayi sizingatheke pamafunika kuchita kupha ndithu. Kugula ndi kugawa yophaipha ndiye kuti sikhalanso idi koma sadaka. Komanso umayenera kupha tsiku lenilenilo kapena masiku atatu otsatira kupanda apo, imeneyonso ndi sadaka odati idi ayi.
Ndiye mwati zidayamba liti? Zidayamba kalekale nthawi ya Abrahamu pomwe Mulungu adamuuza kuti mwezi wa nambala 9, kuyambira pa 1 ndipo tsiku la nambala 10 kuzichitika mwambo oterewu. Kuchoka pa Abrahamu, aneneri onse omwe ankabwera kufikila pa Muhammad amatsatira zimenezi ndiye Asilamu onse amayenera kutsatira.
| 13 |
Botswana Ithetsa Nyumba ya Malamulo Pokonzekera Chisankho Wolemba: Thokozani Chapola .mw/wp-content/uploads/2019/08/masisi-300x168.jpg" alt="" width="514" height="288" />Wathetsa nyumba ya malamulo-President Masisi Mtsogoleri wa dziko la Botswana, Mokgweetsi Masisi wathetsa nyumba ya malamulo, pamene dzikolo likukonzekera chisankho chomwe chichitike mdzikolo mwezi wa October chaka chino.
Malipoti a wailesi ya BBC ati chisankhochi chikhala chovuta kwambiri ku chipani cholamula mdzikolo cha Botswana Democratic (BDP), dzikolo chipezereni ufulu wodzilamulira mchaka cha 1965.
Mtsogoleri wakale wa dzikolo Ian Khama amene anatula pansi udindo wake chaka chatha atalamulira dzikolo kwa zaka khumi wayamba kugwira ntchito ndi chipani chotsutsa kutsatira kusemphana maganizo kwake ndi mtsogoleri wa dzikolo.
Khama wati Masisi yemwe mu nthawi ya ulamuliro wake anali wachiwiri wake, chitengereni udindo wa mtsogoleri wa dziko, wasintha kwambiri zochita zomwe mtsogoleri wakaleyu samayembekezera.
Pa chisankhochi, anthu akuyembekezeka kusankha aphungu a kunyumba ya malamulo ndipo aphunguwa ndi omwe adzasankhe mtsogoleri wa dzikolo.
| 11 |
ACJ Ipempha Atolankhani Achikatolika Asamazibise Wolemba: Sylvester Kasitomu 2019/10/chilanga-170x170.jpg 170w" sizes="(max-width: 337px) 100vw, 337px" />Wamema atolankhani achikatolika-Chilanga Komiti yoyendetsa ntchito za bungwe la atolankhani a achikatolika mchigawo cha ku mmawa kwa dziko lino ya Association of Catholic Journalists (ACJ) yapempha atolankhani onse achikatolika mchigawochi kuti asadzibise koma koma azitenga gawo mmisonkano ya bungwe-li.
Wapampando wa bungwe-li mchigawochi Florence Chilanga wanena izi mboma la Balaka pa msonkhano wakomiti yayikulu yoyendetsa ntchito za bungwe-li.
Chilanga wati bungwe la ACJ linabadwa ndi cholinga choti atolankhani-wa adzigawana luso la udindo umene ali nawo pa ntchito zothandiza kutukula mpingo-wu mmagawo osiyanasiyana, kotero aliyense amene ndi mtolankhani koma ndi wa wa mpingo wakatolika, akuyenera kuchita chotheka polowa ndi kukhala membala wa bungweli.
Mwazina, Chilanga anati nthumwi ku msonkhano-wu zakambirana mfundo zothandiza pa ntchito zokweza ntchito za bungwe-li, komanso momwe bungweli likonzekerere msonkhano wa ukulu wa bungwe-li mdziko muno, umene akonza kuti udzachitikire mchigawo cha ku mmawa kwa dziko lino chaka cha mawa.
Pa mfundoyi adindowa agwilizana zoti msonkhano-wu udzakachitikire mboma la Mangochi pa masiku omwe akonzedwe-wo. Polankhulanso bambo mlangizi wa bungwe-li mu dayosizi ya Mangochi, bambo Harry Mangada anathokoza atsogoleri-wa kaamba kochita mkumanowu.
Iwo analimbikitsa adindo-wa kuti asafooke koma kulimbika pa ntchito zokweza bungwe-li.
Pamenepa bambo Manganda anatsimikizira bungwe-li kuti ofesi yawo ya Communications mu Dayosizi ya Mangochi mogwilizana ya ku Dayosizi ya Zomba ipitiliza kuthandiza ntchito zokuza ndi kufalitsa bungweli mchigawochi.
| 14 |
Gwengwe Akufuna Milandu ya Katangale Izitha Wapampando wakomiti ya kunyumba ya malamulo yowona za ndondomeko ya zachuma Sosten Gwengwe wati magulu osiyanasiyana akuyenera kugwirana manja pa ntchito yolimbana ndi mchitidwe wakatangale mdziko muno.
Tikufuna nkhani tikayiyamba izitha-Gwengwe Gwengwe yemwenso ndi phungu wa kunyumba ya malamulo wa dera la Lilongwe Nsonzi North wauza Radio Maria Malawi kuti kusiyirana komwe kukumakhalapo pa nkhani zakatangale ndi komwe kukuchititsa kuti nkhani zambiri zokhudza katangaleyu zisamaoneke tsogolo lake.
Pamenepa iye wapempha magulu onse okhudzidwa kuti azigwilana manja kuchoka pomwe nkhani yakatangale yayamba mpaka kumapeto kufikira olakwa atalandira chilango.
Ife tikufuna kuti nkhani tikayiyamba izitha bwinobwino mpaka olakwa atalandira chilango choyenera kaamba koti nkhanizi zimakhudza tonse ngati a Malawi ndiye ndi kofunika kuti tigwirizane kuti chilungamo chidziwoneka, anatero Gwengwe.
Mwazina Gwengwe wati ngati mchitidwewu ulekeledwa dziko lino likhalabe likumana ndi mavuto a umphawi kaamba kakusakazika kwa ndalama za boma mosakhala bwino.
| 7 |
OPEZEKA KUMANDA AYANKHA MLANDU Anthu a mmudzi mwa Yesaya Nkosi Mfumu kwa Inkosi Chindi mboma la Mzimba adadzidzimuka ataona galimoto yachilendo itaimitsidwa pamanda a mmudzimo pomwe anthu anayi adali kuchita chizimba kumandako.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Mneneri wa polisi mboma la Mzimba, Gabriel Chiona, adatsimikiza za nkhaniyi ponena kuti iwo adanjata anthu anayi omwe akuganiziridwa mlandu wokhala pamalo popanda chilolezo ndipo iwo adakaonekera kubwalo la milandu la majisitireti Lachinayi pa 20 August.
Chiona adati anthuwo ndi Koloboyi Mwazembe, wa zaka 35, wochokera mboma la Chitipa; Esau Simwimba, wazaka 36, wochokeranso ku Chitipa; Tenson Mhone, wa zaka 65; ndi Chrissy Phiri, wa zaka 73, onse a mboma la Mzimba.
Malinga ndi Chiona, Mwazembe ndi Simwimba alamulidwa kukakhala kundende kwa chaka chimodzi kapena apereke chindapusa cha K90 000 atawapeza olakwa pamlandu wopezeka kumanda popanda chilolezo.
Koma Phiri ndi Mhone adzalowanso mbwaloli sabata ino kuti adzayankhe milandu yopezeka pamalo popanda chilolezo komanso kuba mwachinyengo, milandu yomwe iwo aikana.
Chiona adati anthuwo adanjatidwa pa 13 August pomwe mfumu Msipani Nyirenda adauza apolisi za anthu omwe adali kumanda a mmudzimo.
Malinga ndi Chiona, bambo wina adaona galimo ya oganiziridwawo itaima kwa nthawi yaitali pafupi ndi manda a mmudzimo, zomwe zidamuchititsa kuti akanene za nkhaniyi kwa nyakwawa yemwe adatsina khutu apolisi.
Anthu a mmudzimo adawagwira oganiziridwawo panthawi yomwe amatuluka kumanda. Mmodzi mwa oganiziridwawo adanyamula chithumwa, komanso adapezeka ndi ndalama zokwana K700 000, adatero Chiona.
Msangulutso utafunsa mmodzi mwa oganiziridwawa, Phiri, kuti afokotokoze zomwe ankachitika kumandako, iye adati amafuna chizimba cha bizinesi ndipo chithumwa chomwe adali nacho nchokawira anthu ndalama.
Chithumwachi chimakawa anthu ndalama. Muli njoka yomwe imakhala ikukawa anthuwa ndalamazo, adatero Phiri.
Phiri adati bambo wina adagula njoka kwa singanga, Mhone, yomwe imakawa anthu ndalama koma njokayo idathawa. Iye adati njokayo itathawa iye adaganiza zokagula ina yomwe singangayo adati idali kumanda komwe adapezekako.
Khansala wa derali, Dan Nkosi, adathirira ndemanga za nkhaniyi ponena kuti apolisi adabwera kunyumba kwakwe kudzamutenga kuti akaone zomwe zidachitikazo.
Ndidapeza anthu atawagwira oganiziridwawo kupita nawo kwa mfumu Msipani Nyirenda komwe adafunsidwa zomwe amachita. Iwo adafotokoza kuti amagulitsana chizimba pamtengo wa K700 000 chomwe tidawapeza nacho, adatero Nkosi kuuza Msangulutso.
Mfumu Msipani Nyirenda sadathe kupezeka kuti ayankhulepo pankhaniyi.
| 7 |
Kampani ya AHL Yapempha Alimi Kuti Atsate Ndondomeko Zoyenera Kampani yoyendetsa malonda a fodya mdziko muno ya Auction Holdings Limited yapempha alimi kuti atsate ndondomeko zomwe zayikidwa pa kagulitsidwe ka mbewuyi chaka chino kaamba ka nthenda ya COVID-19.
Wapempha alimi atsatire ndondomeko zoyenera-Ndanga Mneneri wa kampaniyi Tereza Temweka Ndanga wanena izi pamene msika wa malondawa ukuyembekezeka kutsekulidwa lolemba likudzali.
Iye wati pali ndondomeko zatsopano zomwe zayikidwa pofuna kutsatira njira zopewera matenda a COVID-19 kuti alimi ndi onse okhudzidwa asakhale pa chiwopsezo chotenga kapena kufalitsa nthendayi.
Tikugwirisa ntchito ma Receiving Centres kuti alimi azitha kutsatira malonda a fodya kumeneko kudzera mma sellers shit, anatero ndanga.
iwo atinso alimi azithanso kutsatira malonda afodya kudzera mma lamya pa njira ya ahl 252 kwa alimi omwe analembesa.
| 4 |
Kusefukila kwa madzi: Amtauni aiwalidwa? Maso a mabungwe komanso boma ndi anthu onse ali kuchigwa cha mtsinje wa Shire komwe anthu ambiri adakhudzidwa ndi madzi osefukira.
Aliyense amene wapeza thandizo, akumatsetserekera kumabomawa poiwala kuti madera enanso ali pamoto ndikugwetsedwa kwa nyumba zawo.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mwachitsanzo, mumzinda wa Blantyre, anthu ambiri adakhudzidwa ndi ngoziyi koma thandizo lakhala likungopita ku Chilobwe, Chimwankhunda ndi maboma ena monga Mulanje, Thyolo ndi ena akuchigwa cha mtsinje Shire.
Sabata yathayi, bungwe la Self-Help Assistance Program (Asap) mogwirizana ndi IM Swedish Development Partner lidazungulira mzinda wa Blantyre, ukotu ndi kwa T/A Makata komwe adagwidwa tsemwe kuona momwe anthu akuvutikira chifukwa cha ngozi ya madzi.
Anthutu akusowa pokhala ndipo ana angonoangono monga ali pachithunziwa agwidwa njakata chifukwa cha mvula yosaleka yomwe idagwa pa January 11.
Bungweli lidaperekako matani 25 000 a ufa wachimanga, matani 2 500 a nyemba kwa mabanja 540 amene adakhudzidwa ndi ngoziyi.
Banja lililonse lidalandira thumba lolemera makilogalamu 50 a ufa ndi makilogalamu 5 a nyemba. Katunduyu adali wokwana K6.7 miliyoni.
Mkulu wa bungweli Twisiwile Mwaighogha, adati nawonso adali wodzidzimuka kuti anthu ambiri akuvutika motere koma dziko silikudziwa.
| 5 |
Ngakhale ngamba ikuwaula mmera, akuchilimikabe Nkhani ya ngamba siyochita kufunsa chifukwa momwe zikuwaukira mbewu mminda ndiumboni wakuti dzuwa lalanda malo a mvula. Alimi ambiri pano manja ali mkhosi ndipo ena angofika potailatu mtima. Ngakhale zinthu zili choncho, alimi ena sakugonja ndipo akuti sangachoke mmunda pokhapokha ataona kuti mbewu yomalizira yauma ndi dzuwa. Loveness Billy a ku Salima ndi mmodzi mwa alimi olimbika chonchi ndipo STEVEN PEMBAMOYO adacheza naye motere: Escom in free-for-all fuel scam Wait gets longer Secrecy over party funders Mlimiyo pakati pa munda wake wochititsa chidwi Moni mayi komanso ndikudziweni.
Ndili bwino. Dzina langa ndi Loveness Billy ndimachokera mmudzi mwa Mjunga ku Salima.
Tsono pamenepa mukutani? Apa ndikupala udzu mchimanga mwangamu kuti chikule bwino mosanyozoloka chifukwa chosokonezedwa ndi udzu kapena zomera zomwe si gawo la mbewu zanga.
Komatu chimangachi chikuoneka ngati palibepo chomwe mungatole ndi mmene chaumiramu.
Anthu owonanu mukuganiza choncho koma mwini wakene ndikuona kuti chiyembekezo chikadalipo. Mvula itangoti ibwere mukhoza kuona mmene chinganyamukire. Mmene ndikupala chonchimu, zindithandiza kuti chinyontho chochepa chomwe chilipo mnthakamu chigwire ntchito ku mbewu zokha osati kulimbirana ndi udzu.
Mesa boma likuti ndi mmene zinthu zililimu mukuyenera kukangalika ndi mbewu zina zopirira ku ngamba? Zimenezo tikutsatiranso moti chakumunsi kwa mindayi kuli madimba komwe tagaula kale ndipo pompano tikabzalako mbewu zinazo monga nyemba, kachewere, mbatata ndi chinangwa. Chinangwacho ndiye tidabzala kale koma pano tikufuna kukabzala mbatata chifukwa timasakasaka mbewu ndiye yapezeka.
Alimi anzanutu atambalala kusungira mphamvu kuti mvula ikagwanso adzaunde mizere ya mbatata kapena chinangwa.
Ayi amenewo ndiwosamvetsa chabe chifukwa ngakhale a bomawo sakunena kuti tizule kapena kunyanyala chimanga koma kuti pambali pa chimangacho tibzalenso mbewu zina. Palibetu vuto kusakaniza mbewu zinazo ndi chimanga makamaka pomwe malo ali ochepa. Mwachitsanzo, munthu akhoza kubzala mbatata mmphepete mwa mzere wa chimanga. Chimanga chikakula pangono amatenga mbewu ya mbatata nkubzala ndipo zonse zimakula bwinobwino.
Inu mumachitaponji pa zaulimi wa mthirira? Ulimi umenewonso timapanga mchilimwe. Tidakumba madamu okololeramo madzi omwe timagwiritsa ntchito kuonjezera omwe timapatutsa mumtsinje chifukwa mtsinjewo pena madzi amachita kutheratu nanga ogwiritsa ntchito si ambiri kuyambira kumtunda komwe udachokera mpaka kumunsi.
Mwakonzekera bwanji ulimi wa mthirira? Pakadalipano tikuyanganabe zipangizo zina makamaka mbewu ndi feteleza koma zina monga madzi ndi muja ndafotokozera kale kuti kupatula mumtsinje, tili ndi madamu okololera madzi. Ikakhala ntchito ina monga kugaula ndi kuunda mizire ziri mkati mmadimba ena pasi pakadali pofewa.
Kugawuliratu pano ndiye podzafika chilimwe sipadzakhala patalimbaso? Ayi timalawirira kukatchefula mvula ija ikangotha pansi pakayamba kuchita mbuuu. Siyikhalanso ntchito yowawa komanso tikatero timadzipatsa mpata wokwanira wothira manyowa kuti ndi chinyontho chija, dothi ndi manyowawo zilowererane bwino.
Inu mungawauze chani alimi anzanu omwe ataya mtima? Asataye mtima koma akhale ndi chikhulupiliro zonse zidzakhala bwino. Vuto ndilakuti akatambalala, pomwe mvulayi idzabwerenso adzakhala ndi chintchito chachikulu. Chofunika nkungosamala mbewu zomwe zidamera kalezi nanga sipadalowa kale zambiri. Mvula ikadzabweraso tizidzangopakiza momwe mbewu zaferatu.
| 4 |
Makhwala Ozunguza Ubongo Akukoledzera Uphawi Kwa Achinyamata-RAC Wolemba: Sylvester Kasitomu Kukula kwa mchitidwe wogwilitsa ntchito makhwala ozunguza bongo ndi kumwa mowa mwauchidakwa Drug and Alcahol Abuse akuti ndi umene ukukolezera mavuto a umphawi ndi makhalidwe oyipa pakati pa achinyamata ambiri mdziko muno.
Mkulu wa bungwe lopereka uphungu wa za maufulu a wanthu la Rights Advice Center RAC a Madalitso Masache ndi amene wanena izi pakutha pa maphunziro a tsiku limodzi a atsogoleri a zipembedzo ndi adindo ena mboma la Mangochi.
Malingana ndi a Masache maphunziro-wo anali othandiza atsogoleri-wa za momwe angathandizire pa ntchito zolimbana ndi mchitidwe-wu mbomalo ndipo anachitika ndi thandizo lochokera ku bungwe la Norwegian Church Aid NCA.
Tinabwera kudzawaphunzitsa anthu amawatumikira ku madera kwawo kuti akawafikire anthu amene akupezeka mmadera awo kuti mchitidwe ogwiritsa ntchito mankhwala ozunguaza bongo kaamba koti izi ndimene zikubwezeretsa chitukuko cha dzikolino mbuyo, anatero Masache.
Ndipo polankhulanso mmodzi mwa omwe achita nawo maphunziro-wo Sheikh Abdula Kaposa anayamikira bungwe-li kamba ka maphunziro-wo kaamba koti dera lawoli likukhudzidwa kwambiri ndi mavuto omwe akudza pakati pawo kaamba komwa mowa mwauchidakwa.
Chomwe chimachitika nchoti munthu akagwiritsa ntchito makhwala ozunguza bongo monga kumwa mowa mwauchidakwa amachita zinthu zosayenera monga mchitidwe ogonana zomwe zikuchulukitsa chiwerengero cha anthu omwe akudwala matenda oapatsirana pogonana monga edzi, anatero Sheikh Kaposa.
Maphunzirowa anasonkhanitsa adindo ozungulira boma lamangochi omwe anagakhale ndi kuthekera kophunzitsa anzawo za kuyipa kogwiritsa ntchito mkhwala ozunguza ubongo.
| 14 |
Papa Wapemphelera Anthu Amene Ntchito Zawathera Kaamba ka Coronavirus Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wati ndi wokhudzidwa ndi anthu ambiri omwe ntchito zawo zatha kaamba ka mliri wa Coronavirus.
Papa walankhula izi lolemba pa Misa yomwe anatsogolera ku likulu la mpingowu ku Vatican.
Iye wati mliri wa Coronavirus wachititsa kuti anthu ambiri azivutika chifukwa choti ntchito zawo zatha.
Mliri wa Coronavirus wabweretsa mavuto a nkhaninkhani kaamba koti malo ambiri a ntchito mmaiko osiyanasiyana sakuchita malonda kapena kupeza phindu mmene zikhalira nthawi zonse ndipo chifukwa cha ichi malo antchitowa akhala okakamizidwa kuchotsa ntchito anthu awo ena ogwira ntchito.
Iye wati ndi wokhudzidwa akaganizira anthu ambiri omwe ntchito zao zatha malinga ndi mavuto omwe mliri wa Coronavirus wabweretsa mmalo ambiri ogwirira ntchito.
Pa chifukwa ichi Papa Francisco wapempha anthu onse kuti alumikizane naye popempherera anthu omwe akusowa ntchito chifukwa ntchito zao zatha ndipo chifukwa cha ichi miyoyo yao ikuyenda mwa pendapenda chifukwa cha vuto la ndalama.
Ku Malawi mliriwu wagwedezanso popeza malo ogwirira ntchito akhudzidwa ndi mliriwu. Mwachitsanzo sukulu zambiri zomwe si za boma zikuvutika kulipira aphunzitsi kaamba koti sukuluzi zimadalira ndalama zomwe ana amalipira kuti zithandize kulipira aphunzitsi koma padakali pano sukulu zonse ndi zotseka kaamba ka mliri wa Coronavirus.
| 13 |
Bajeti sidaganizire anthu akumudzi Ali ndi mwana agwiritse, akutero amabungwe ati poti ndondomeko ya boma ya chuma ya chaka cha 2012 mpaka 2013 inayenera kulingalira bwino zochepetsera munthu wakumudzi ululu wa kugwa kwa ndalama ya kwacha.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Izi aunikira ndi mkulu wa bungwe loona ufulu wa ogula la Consumers Association of Malawi (Cama), John Kapito, mphunzitsi wa zachuma ku sukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, Ben Kaluwa, mafumu ndi anthu ena msabatayi.
Apa nkuti aphungu ena ku Nyumba ya Malamulo atandaulanso ndi ndondomekoyi pomwe inaperekedwa ndi nduna ya zachuma, Dr Ken Lipenga, mnyumbayo Lachisanu sabata yatha kuti aphungu ayambe kukambirana.
Ndemangazi zalunjika poti ndondomekoyi ikomere akumudzi omwe achulukira malinga ndi kalembera wa anthu wa 2008.
Kalemberayo adaloleza kuti chiwerengero cha anthu mdziko muno chili pafupifupi 13 miliyoni.
Mwa chiwerengerochi, pafupifupi anthu 84 mwa 100 alionse amakhala kumudzi ndipo 16 otsalawo ndi amene ali mmatauni ndi mmizinda.
Mavuto akulu Kapito wati malinga ndikugwa kwa ndalama ya kwacha, moyo wa anthu akumudzi uli pamoto.
Boma lachotsa msonkho pa nyuzipepala, buledi ndi kaunjika koma mutha kuwona kuti izi ndi za anthu a mtawuni mokha, osati a kumudzi.
Njira yopulumutsira munthu wakumudzi ndi kumupatsa maganyu opezerapo kangachepe, watero Kapito.
Iye watinso boma likuyenera kukhazikitsa njira zoti katundu kumudzi asamakwere moboola mthumba.
Kaluwa wati boma langoika chidwi pa anthu a mmizinda ndi mmatauni ndipo nkoyenera lichitepo kanthu pa madandaulowo a akumudzi.
Mbali ya zamaphunziro ndi ya zipangizo zotsika mtengo ndikomwe ndikuona ngati ndondomekoyi yaserapo kuthandiza wakumudzi.
Lolemba lathali, aphungu a ku Nyumba ya Malamulo adapemphanso boma kuti likhazikitse njira zothandizira anthu a kumudzi.
Mneneri wa zachuma kuchipani cha MCP, Joseph Njobvuyalema, anati boma laika patsogolo munthu wa mtauni, osati wakumudzi.
Zipangizo zaulele Njobvuyalema wati boma lidakaonetsetsa kuti ndondomekoyo ikupatsa munthu wakumudzi ntchito kapena ganyu kuti atha kupeza ndalama.
Kugwa kwa ndalama ya kwacha ndi pafupifupi ndi theka la mphamvu zake ndi vuto lalikulu kwa munthu wakumudzi chifukwa zinthu zidakwera pomwe iye alibe pogwira, adatero Njobvuyalema.
T/A Phambala ya mboma la Ntcheu yati ngakhale ndondomekoyi ya chaka chino yaikabe ndondomeko ya zipangizo zotsika mtengo, komabe wati boma lichite kanthu pofewetsa moyo wa munthu wakumudzi.
Iye wati boma likuyenera lipitirize ndondomeko ya nthandizi yomwe akuti ndiyo ingapindulire anthu akumudzi.
Otenga nawo mbali pantchito za pansi pa ndondomeko ya nthandizi amalipidwa pomwe agwira ntchito. Patsiku amalandira amalandira K200.
Boma liganizire zobweretsanso ndondomekoyi komanso kukweza malipiro kufika pa K400, watero Phambala.
Mfumu Yaikulu Themba Chikulamayembe ya mboma la Rumphi yati kumudziko zinthu zakwera mtengo kotero boma liike njira zoti anthu akumudzi athandizike.
Bajeti isinthe miyoyo Mary Jimu wa mboma la Chikhwawa kwa T/A Mulolo wati anthu akumudziko avutika chifukwa ndondomekoyi sidasinthe moyo wawo.
Tili ndi mabungwe kumudzi kuno, bwenzi boma litaika ndalama mmabungwemo kuti azithandizira anthu akumudzi kuno.
Titha kumapeza ngongole kapena ntchito zakumudzi. Koma momwe zilili moyo ukhala wovutirako, adatero Jimu.
Thoko Loga yemwe amathira utoto galimoto ku Chilinde mumzinda wa Blantyre wati mndondomeko ya zachumayo mulibe chawo.
Ntchito zikusowa. Maso a boma akhale pa anthu omwe saali pantchito chifukwa zinthu zakwera mtengo. Yemwe sakugwira ntchito akugulabe zinthuzo pa mtengo wokwerawo, adatero Loga.
Koma Mneneri wa boma, Moses Kunkuyu, wati ndondomekoyi yayesetsa kufungatira akumudzi. Iye watinso anthu asaiwale kuti ndondomekoyi ya chaka chinoyi ndi yofuna kukonza chuma chomwe pakatipa sichimayenda bwino.
Iye wati mndondomekoyi muli zina zomwe zingapindulire munthu wakumudzi monga ndalama zomwe zalowa mgawo la chitukuko cha kumudzi ya Social Cash Transfer.
Tikati kukonzanso sikutanthauza kuti mukukonza mtauni mokha ndikusiya kumudzi. Zilipo zambiri zopindulira munthu wakumudzi.
Mwachitsanzo, kuchotsa misonkho pa buledi ndi zina zipindulira munthu wakumudzi, adatero Kunkuyu.
Anthu enanso anayamikira kale ndondomeko ya chaka chino yomwe ndi ya K406 biliyoni kusiyana ndi ya chaka chatha ya K394 biliyoni.
Unduna wa zamaphunziro walandira K74 biliyoni yomwe ndi yochuluka kuponsa maunduna ena onse.
Chaka chatha undunawo unali ndi K54 biliyoni.
Unduna wa zaulimi walandira K68 biliyoni yomwe K40 biliyoni ndi ya zipangizo zotsika mtengo.
| 11 |
Zizindikiro za kufa kwa ziwalo Dotolo wa pa chipatala cha Gulupu mboma la Blantyre, Lerato Mambulu, wati kufa kwa ziwalo nthawi zambiri kumachitika mwadzidzidzi.
Pachifukwa ichi, kumakhala kovuta munthu kumva kapena kuonetsa zizindikiro zoti afa ziwalo.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Munthu amatha kungomva kupweteka mutu ngati amumenya mwina ndi chitsulo ndikugwa pansi basi kufa kwa ziwalo nkukhala komweko, iye adatero.
Mambulu adafotokoza kuti izi zimachitika kwa anthu amene misempha yawo ya magazi yaphulika mbali ya thupi yomwe yafayo.
Iye adati misemphayi ikaphulika, magazi sayenda kupita ku ubongo zotsatira zake sipakhala kulumikizana kulikonse pakati pa ubongo ndi mbali yomwe sikukufika magaziko.
Dotoloyu adati zinthu zikafika pamenepa mbaliyo imaleka kugwira ntchito.
Anthu ena amatha kufa ziwalo kapena kusiya kuyankhula kwa maola ochepa okha ndikuchira. Ichi ndi chizindikiro chachikulu cha matendawa, iye adatero.
Mambulu adati izi zili chomwechi chifukwa anthu oterewa amakhala pachiopsezo chachikulu choti atha kuzakhala ndi vutoli mokhazikika mtsogolo.
Pachifukwa ichi, dotoloyu adati munthu akaona izi, asazitenge mwa chizolowezi kuti ndi momwe ndimachitira, koma athamangire ku chipatala kukapeza thandizo kuti mtsogolo, lisadzakhale vuto lokhazikiza.
Iye adati ngakhale izi zili chomwechi, ndi anthu ochepa okha omwe amatha kuyamba motere.
Kwa anthu omwe BP yawo imakhala yokwera ndipo amamva kuwawa kwa mutu kwambiri, nkhope imatha kuonetsa zizindikiro zofooka kusonyeza kuti nthawi ina iliyonse, ziwalo zikhoza kufa, iye adatero.
Tsabata ya mawa tizafotokoza zinthu zomwe zimamuika munthu pa chiopsezo cha matenda a kufa kwa ziwalo.
| 6 |
Jooma wati Mangochi Ikutsalira pa Chitukuko By Thokozani Chapola ent/uploads/2019/07/jooma.jpg" alt="" width="512" height="276" />Jooma: Dera la Katuli ndi lotsalira kwambiri pa chitukuko Jooma Nduna yowona za mtengatenga ndi zomangamanga Ralph Jooma wati Mangochi ndi limodzi mwa maboma amene akutsalira mmbuyo kwambiri pa nkhani za chitukuko.
Jooma amalankhula izi pa sukulu ya pulamimale ya Katuli mdera la kumvuma kwa boma la Mangochi komwe phungu wa kunyumba ya malamulo watsopano wa derail Francesca Masamba Theula amachititsa msonkhano wothokoza anthu pomuvotera, yemwe watenga udindowu kuchoka kwa Abubakar Mbaya wa chipani cha UDF yemwe wakhala phungu wa derali kwa zaka 25.
Pamenepa Jooma walonjeza kuti boma limanga nsewu wa Mangochi-Katuli ndi cholinga chofewetsa vuto la mayendedwe lomwe anthu a mderali amakumana nalo.
Dera lino lili ndi sukulu imodzi yokha ya sekondale, kuli mavuto a madzi komanso nsewuwu suli bwino. Ngati boma nsewu umenewu tawuyika kale mu maplan athu kuti tiyike phula, anatero a Jooma.
Mmawu ake phungu wa derali Francesca Masamba Theula anati anawona kuti ndi kofunikira kwambiri kuti apitenso ku derali ndi kukathokoza anthu amene anamusankha pa udindowu.
Kuti ineyo ndikhale pa udindowu ndi chifukwa cha voti yawo. Panali ena achikulire oti anavutikira kuyenda mpaka kuzandivotera choncho ndinawona kuti ndi kofunika kuti ndizawathokoze mapadera; tidye, timwe ndi kusangalala limodzi, anatero Masamba.
Mu zokambirana za nyumba ya malamulo zomwe zapitazi Masamba analankhulapo kuti yemwe anali phungu ku dera lake palibe chomwe anachitako ku mbali ya chitukluko zomwe zinakwiyitsa a mbali yotsutsa boma maka a chipani cha UDF pomwe phungu wadera la Mangochi Malombe a Misolo Mussa Kapichira anayimilira ndi kudzudzula zomwe zinayankhulidwazi.
Ena mwa mwe anali nawo pa mwambo wothokozawu ndi phungu wad era la pakati mboma la mangochi Victoria Kingstone komanso phungu wa dera la Mangochi Masongola Ishmael Grant yemwe anapambana ngati woyima payekha koma tsopano walowa chipani cha DPP.
Pa tsiku lomwelo Masamba anachititsanso misonkhano ya mtunduwu ku Iba komanso Makanjira mderalo.
| 14 |
Khansala Adzipereka Pofuna Kutukula Dera Lake Wolemba: Sylvester Kasitomu Khansala wa dera la Mbedza mu mdzinda wa Zomba Steven Bamusi wati adzipereka pa ntchito zotukula delaro Khansala Bamusi yemwe ndi wachipani cha DPP waudza Radio Maria Malawi kuti iye ali wokonzeka kugwira ntchito ndi munthu wina aliyense pofuna kuthandiza pa ntchito zokweza delaro.
Pamenepa Iye wapemphanso phungu wa mu mdzinda-wu kuti alimbikitse mgwilizano wabwino ndi makhansala onse omwe akutumikira madera ena a mu mdzindawu, ndi cholinga choti athandize pa ntchito zokweza mdzinda-wu.
Tili ndi ntchito yayikul yoti tiigwire mu teremu imeneyi monga kumanga misewu ngakhale ina yamangidwa monga nsewu ochokera pa adho kukafika mpotola school anatero Bamusi.
Mwazina iye wathokoza boma la DPP kaamba koyambitsa ndondomeko yokonza misewu mmizinda monse komanso kuonetsetsa kuti madzi abwino akupezeka mmizinda yonse.
Khansalayu wasakhadwa kwa chiwiri tsopano kuchokera mu chisankho chomwe chinachitika mchaka cha 2014 ndipo athi agwira limodzi ndi phungu wakunyumba yamalamulo yemwe wangosankhidwa posachedwapa a Bester Awali.
| 14 |
Papa Wapereka Ambulance kwa Anthu Ovutika Mzinda wa Rome Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wapereka galimoto ya mtundu wa Ambulance kuti izitumikira anthu osauka ndi osowa pokhala.
Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican Papa wapereka galimoto ya mtundu wa ambulanceyi lamulungu pa 31 May, 2020.
Galimoto ya mtundu wa ambulanceyi izithandiza popereka chithandizo cha chipatala kwa anthu osauka komanso osowa pokhala omwe amapezeka atagona mmisewu ya mu mzinda wa Rome.
Galimoto ya mtundu wa ambulanceyi yomwe ndi ya makono yokhala ndi zipangizo za chipatala izithandiza popereka thandizo la msangamsanga la chipatala kwa anthu osauka ndi osowa pokhala omwe kawiri-kawiri amapezeka atagona mmisewu ya mu mzinda wa Rome.
Papa Francisco anadalitsa galimoto ya mtundu wa ambulanceyi asadaipereke kwa Cardinal Konrad Krajewski yemwe ndi mkulu woyendetsa ntchito za chifundo za Ofesi ya a Papa ndipo amatchulidwa kuti Papal Almoner mchingerezi.
Malinga ndi kalata yomwe likulu la Mpingo wa Katolika latulutsa, galimoto ya mtundu wa ambulanceyi aipatsa kale malembo oti SCV kuimira kuti Vatican City State kusonyeza kuti ndi imodzi mwa galimoto za kulikulu la Mpingo ku Vatican.
Galimoto ya mtundu wa ambulanceyi aipatsa dzina la Modesta Valenti yemwe adamwalira pa 31 January 1983. Iye anali mzimayi yemwe adalibe pokhala ndipo anali kugona mmisewu ndipo pa tsiku lomwe adamwalira anali atadzidzidwa kwambiri ndipo amasowa chithandizo cha kuchipatala. Anthu ena omwe adali mgalimoto ya mtundu wa ambulance ina adakana kumuthandiza ati chifukwa anali ndi nsabwe.
| 6 |
Papa Wapempha Akhristu Akhale Odekha Mtsogoleri wa Mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisko wapempha akhristu kukhala odekha ndi oleza mtima.
Papa Francisko walankhula izi lachitatu kulikulu la Mpingo wa Katolika ku Vatican.
Iye wati kukhala wodekha kumabweretsa chiyanjano pakati pa anthu pamene mkwiyo umabala chisokonezo komanso kugawikana.
Pamenepa iye wapempha akhristu kukhala odekha, achifundo ndi achiyembekezo nthawi zonse.
Papa Francisko wati kukhala wodekha pamene zinthu zili bwino nkosavuta koma iye wati kukhala wodekha pamene zinthu zathina ndiye mayeso aakulu.
Pamenepa Papa Francisko wati Yesu Khristu ndiye chitsanzo cha munthu wodekha yemwe ngakhale adakumana ndi masautso aakulu adapitirira kukhalabe wodekha.
Mwazina papa wati anthu odekha amakhala ndi abwenzi ambiri kusiyana ndi anthu a mkwiyo choncho nkofunika kuti akhristu akhale anthu odekha ndi oleza mtima.
| 14 |
CADECOM Ipindulira Anthu a Mboma la Mwanza By Glory Kondowe Mpingo wakatolika mdziko muno wati ndi wokhutira ndi mmene anthu a mboma la Mwanza akupindulira ndi ntchito zake zomwe zikugwiridwa ndi bungwe lake la zachitukuko la Catholic Development Commission in Malawi (CADECOM).
Mlembi wamkulu ku bungwe la ma episikopi a mpingo wakatolika mdziko muno la Episcopal Conference of Malawi (ECM), bambo Henry Saindi alankhula izi pambuyo poyendera ntchito zosiyanasiyana zomwe bungwe la CADECOM likugwira mdera la mfumu yaikulu Kanduku mboma la Mwanza mu archdayosizi ya Blantyre. Bambo Saindi ati kudzera mu ntchitozi zawonetsa poyera kuti anthu a mderali akuthandizika mu njira zosiyanasiyana kamba koti akutha kuzipezera okha zosowa za moyo wawo wa tsiku ndi tsiku.
Ayamikira bungwe la CADECOM bambo Saindi Pamenepa Iwo ati mpingo-wu upitiliza kugwira ntchito ndi boma pothandizira ntchito zotukula dziko lino.
Ntchito zomwe bungwe la CADECOM ikuwathandiza anthu amudzi mwa Ulemu ndi monga kuwathandiza kufetsa ndikuwokera mitengo okha komaso azimayi akuwaphunzitsa bizinesi yophika mowa wa wine womwe ukupangitsa kuti njira yopenzera chuma isamasowe, anatero bambo Saindi.
Iwo ati ndi okhutira ndi bungwe la CADECOM lomwe limathandizidwa ndi abwenzi ochokera mdziko la Australia lomwe cholinga chake ndikuona zomwe anthu akuchita kale ndi kuwathandiza pomwe sangathe kufikilapo monga ulimi osiyanasiyana.
| 14 |
Adakumana bwanji mchakacho? Ankadzapepesa maliro a mkazi wanga Ukwati ndi chinthu chabwino, ndipo Mulungu amasangalala nacho. Chaka cha 2015 Mulungu adadalitsa ena ndi mabanja ndipo lero tingochita molawitsa mwa ochepa amene adalandira madalitso olowa mbanja.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Precious ndi Kachingoni kake patsiku la chinkhoswe Tiyambe ndi Excello Zidana amene adakumana ndi nthiti yake Katerina Mtambo kudzeranso mmphamvu ya Mulungu.
Zidana, mkonzi wa pologalamu ya Ulimi Walero ku MBC, adakumana ndi nthiti yakeyi malo angapo koma nthawi yeniyeni idali pamene Katerina amakapepesa Excello pa imfa ya mkazi wake.
Katerina adataya wokondedwa wake chimodzimodzinso Excello. Awiriwa akuti adapepesana za imfayo koma kumapeto kwake adatolana ndi kumangitsa woyera.
Kudali kosoketsa nsapato Wina waluso pakapezedwe ka namwali ndi Richard Chipuwa, goloboyi wa Be Forward Wanderers.
Kuonongeka kwa nsapato ya Chipuwa udali mwayi, poti pokakonzetsa nsapatoyo adakabatha namwali yemwe adapangitsa naye chinkhoswe mchaka changothachi.
Kukumanako akuti kudali kosavuta koma kuti asoke Chichewa chokhetsa dovu la Dinnah Hxaviel ndiye idali ntchito yoposa kukhala pagolo.
Ngakhale mayi a njoleyi amaletsetsa mwana wawo kuti asayerekeze kuyenda ndi anyamata, koma nthawi idakwana kutinso makolowo sakadakwanitsa kuletsa pamene adakumana ndi mwamuna weniweniyu.
Adali kasitomala wanga wa tchipisi Wina ndi Steve Nthala yemwe ndi mkulu wa nyimbo mgulu la Area 36 Anglican Choir ku Lilongwe amene adapeza njole yomwe idali kasitomala wake wa tchipisi.
Iye akuti adagwa mchikondi ndi Chrissy Malipa yemwe adali kabwerebwere wa tchipisi chomwe mnyamatayu ankakazinga pachiwaya.
Steve akuti namwaliyu amati akamadzagula tchipisi pachiwaya chake mtima umagunda ndipo amangomuyezera chambiri. Chidali chiyambi mgwirizano wolowa mbanja.
Timakayangana osewera mpira ku Kasungu Ulendo wa timu ya Surestream wokayangana osewera mboma la Kasungu udali waphindu kwa Team Manager wa timuyi Honest Nkhwazi.
Honest adapeza chamwayi kuti asodzekonso Chisomo Nkhoma, yemwe ndi wapolisi papolisi ya Kasungu kuti akhale wachikondi wake. Sadaope yunifomu ya polisi, pali chikondi palibe mantha.
Awiriwa adachititsa chinkhoswe mboma la Kasungu ndipo amangoyembekezera kuti ukwati tsopano uchitike, abusa agwire ntchito yodalitsa awiriwa.
Awa ndi ochepa chabe amene tidawatulutsa patsamba lino kutifotokozera omwe adakumanirana ndi okondeka awo. Mchakachi achite mphumi ndani? Dzina la Yesu ndilo lidachititsa Akulu adati dzina limapereka kapena kulanda mwayi wa munthu ndipo izi nzoonadi, taonera pa Noel Nthala, yemwe mumzinda wa Lilongwe amadziwika ndi dzina lakuti Yesu ndipo ndi mmodzi mwa masapota akuluakulu a timu ya Silver Strikers.
Anthu ambiri mumzinda wa Lilongwe amakhala ndi chidwi akamva za Yesu poganiza kuti mwina ndiye wa ku Yerusalemu ndipo ichi ndicho chidatchukitsa mnyamatayu yemwe pano wapeza nthiti Zuziwe Nyondo.
Kukumana kwa Nthala ndi Zuziwe mwina sikungadabwitse chifukwa monga anthu ambiri mumzindawu amazizwa ndi dzinali nkutheka namwaliyu naye amafunitsitsa atamuona.
Ndimamuona ndikamachokera kuntchito koma tsiku lina nditalimba mtima ndidamuimitsa nkumulonjera. Nditamuuza dzina langa adaoneka wodzidzimuka koma ine sindidatengere zimenezo, mtima wanga udali pa iyeyo basi, adatero Nthala.
Naye Zuziwe adati dzina lokhalo amangolimva koma samadziwa kuti munthu wake nkukhala mmene amawonekera Nthala, ayi.
| 15 |
Maudindo ayamba kuchucha mboma Pomwe mtsogoleri wa dziko lino yemwe wangosankhidwa kumene Lazarus Chakwera wayamba kusankha adindo mbom, ku Nyumba ya Malamulo zinthu zasadabuzika.
Chakwera adayamba nkusankha nduna zisanu zomwe ndi wachiwiri wake Saulos Chilima ngati nduna ya mapulani a zachuma ndi woyanganira za ogwira ntchito mboma, Felix Mlusu ngati nduna ya zachuma.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Adakana unduna: Msishakuchoka Iye adasankhanso Richard Chimwendo Banda ngati nduna ya chitetezo cha mdziko komanso Modecai Msisha ngati nduna ya za malamulo ndi chilungamo ndinso Chikosa Silungwe ngati mlangizi wamkulu wa boma pa malamulo. Koma Msisha adakana udindowo.
Pambali pa awa, Chakwera adasankhanso Prince Kapondamgaga ngati woyanganira ogwira ntchito ku nyumba ya boma, Zangazanga Chikhosi ngati mlembi wamkulu wa boma komanso Janet Banda ngati wachiwiri wake.
Chakwera adati pali chikonzero choti asankhe nduna zosaposa 30, pomwe nduna zosachepera 12 zikhale amayi.
Ku Nyumba ya Malamulo nako kudachitika pelete pomwe omwe adali kutsogolo, lero ali kumbuyo ndipo omwe atsogolera, pano akutsatira.
Maudindo mnyumbayo adasintha moti yemwe adali mtsogoleri wa nyumba yonse Kondwani Nankhumwa pano ndi mtsogoleri wa mbali yotsutsa boma pomwe Chimwendo Banda yamwe adali mbali yotsutsa boma pano ndi mtsogoleri wa nyumba yonse ndipo akukhala mpando oyambilira mnyumbayo.
Bright Msaka ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa DPP Nankhumwa, Simon Vuwa Kaunda ndi wokhazikitsa bata kumbali ya DPP pomwe Mary Navicha ndi wachiwiri wake.
John Chikalimba ndi mtsogoleri wa chipani cha PP, Noah Chimpeni ndi okhazikitsa bata ku mbali ya PP pomwe Ackson Kalaile Banda ndi wachiwiri kwa Chimpeni.
Tsopano nyumbayi ikukonzekera zosintha utsogoleri wa makomiti ena kuti zigwirizane ndi momwe malamulo akagwiridwe kantchito mnyumbayo amanenera. Malinga ndi malamulowo, apampando a makomiti sayenera kukhala ochokera kuchipani cholamula choncho makomiti onse amene wapampando ndi wachipani cha MCP tsopano asintha.
Chimwendo Banda adati ngati mtsogoleri wa nyumba yonse, aonetsetsa kuti aphungu akutsatira malamulo a nyumbayo komanso kuti zochokera mnyumbayo zizikhala zokomera anthu.
Paja nkhani ndi ya tsogolo lowala ndiye kuwalako kukuyenera kuyambira kwa adindo ngati ife choncho ndionetsetsa kuti ndigwire ntchito ndi aphungu onse kuti titumikire Amalawi, adatero Chimwendo Banda.
| 11 |
Mafumu a ku Zambia akulowerera kwa Mkanda Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Pamene nkhani ya mpungwepungwe wa nyanja ya Malawi pakati pa dziko lino ndi la Tanzania ili mkamwamkamwa, nawo mafumu ena a dziko la Zambia ali pakalikiriki kugawira anthu awo malo mbali ya dziko lino kwa mfumu yaikulu Mkanda mboma la Mchinji.
Malinga ndi mfumu yaikulu Mkanda, mkangano wa malo kumalire a dziko lino ndi Zambia udayamba zaka za mma 1970.
Mkanda adauzaTamvanimsabatayi kuti kuchokera mzakazi kumaloku kwakhala kukufika akuluakulu a boma ochokera ku Chipata mdziko la Zambia, Blantyre ndi Lilongwe kukakambirana zothana ndi mpungwepungwewu.
Mchaka cha 1998 kapena 1999 kudabwera anthu aboma kudzakambirana, koma vutoli likadalipo ndithu; akugulitsa malowa ndi Chanje komanso Mkandamateyo yemwe ndi mwana wa a agogo yemwe adatsalira ku Zambia nthawi ya chitaganya cha Rhodesia ndi Nyasaland, idatero mfumuyi.
Iyo idati mfumu Chanje yalowerera maesiteti ochulukirapo a Mpale, Chimwamkango, Chimwemwe, Mthyolasenje ndi Chankhungu pomwe Mkandamateyu amamvetsa ndi kusiya kulowereraku akauzidwa kutero.
Kuno milandu ya malo simatha, timangokhalira kukangana ndi anzathu a ku Zambia omwe ativutitsa kwabasi, iwowa sakulemekeza mabikoni omwe adaikidwa kumaloku, Mkanda adatero.
Iye adati izi zakhudza anthu ake omwe akusowa malo olima.
Polankhulapo pankhaniyi, DC wa boma la Mchinji, Yamikani Chitete, adati ofesi yake yakhala ikulandira madandaulo kuchokera kwa eni maesiteti omwe alowereredwawa.
Mwezi wa May kunabwera anthu kudzadandaulanso za nkhaniyi ndipo tinawauza kuti tifikako mavoti a patatu akadutsa, choncho ine ndi anzanga a ku Chipata tipitako Lachisanu [dzulo], Chitete adatero.
Bwanamkubwayu adati mmbyomu kumaloku kudapitidwanso pamodzi ndi bwanamkubwa wa boma la Chipata ndipo atawalankhula anthuwo adachoka mokakamizidwa ndi apolisi a dzikolo.
| 11 |
Vuto La Madzi Lakula Ku Nkhotakota Wolemba: Glory Kondowe Anthu okhala ku dera la Liwaladzi kwa mfumu Kulinji mboma la Nkhotakota loweruka apempha boma kuti liwaganizire powapatsa madzi aukhondo kuti miyoyo yawo ikhale yabwino.
Anthu okhudzidwawa ati ngakhale kuti boma la Nkhotakota lili mphepete mwanyanja ya Malawi, koma anthu ambiri akukumana ndi mavuto kuti apeze madzi abwino mosavuta edby="caption-attachment-9652" class=" wp-image-9652" src="http://www.radiomaria.mw/wp-content/uploads/2019/09/mhone-chanjo.jpg" alt="" width="576" height="383" />Chanjo Mhone: Tikukambirana ndi a VDC Kwathawi yayitali takha tikugwiritsa mijigo koma chifukwa chakuchulukana kwa anthu ndimijigo yomwe inaparekedwa yachepa, anatero mayi Christina Kapalamula omwe ndi mmodzi mwa anthu okhudzidwa.
Mmodzi mwa abambo okhudzidwa a Stefano Joseph anati iwo ndi wokhudzidwa ndi vuto la madzi chifukwa akazi awo amalawilira kwambiri ndikupita kokasaka madzi.
Tikumakhala ndi nkhawa chifukwa zikhodza kuyika miyoyo yawo pachi wopsezo, anatero a Stephano.
Mai Martha Mhone yemwe ndi phungu wa delari wavomeleza kuti vutoli ndilalikulu mudelari ndipo iye anachita changu ponena kuti komiti yowona zachitukuko la VDC lichitapo kathu.
Tagwiriza ngati nyumba ya chitukuko timatulako ndalama kuti mijigo ina yomwe boma linakumba ndiyeno tinapanganaso kuti tigawa malire kuti mijigo izikhara pakati pamudzi osati panyumba yamunthu cholinga kuti anthu zaipindulapo, anatero Mhone.
| 6 |
Anatchezera Ndikufuna sukulu Zikomo Anatchereza, Ndine msungwana wa zaka 19. Sindidakwatiwepo, ngakhale sukulu ndidaisiyira Fomu 1 zaka zutatu zapitazo.
Sukuluyo ndidasiya chifukwa chosowa ndalama chifukwa makolo anga adasiyana ndipo sangathe kundithandiza.
Padakali pano ndikugwira ntchito mnyumba ya munthu. Izi ndidapanga chifukwa anthu amandiuza kuti ndikwatiwe koma ine sindimafuna zimenezo. Ndimafuna kudzakwatiwa ntakonza tsogolo lowala.
Chikundivuta ndi nkhani imene ndili nayo patsogolo langa. Nditani kuyi tsogolo langa likhale lowala.
MN, Thyolo.
MN, Ndathokoza polemba uthenga wanh wogwira mtima. Ndihamike chifukwa cha luntha lanu pofuna maphunziro. Si asungwana ambiri amene ali paumphawi amene amaganiza momwe mukuchitiramu.
Si zoona kuyi kulowa mbanja ndiye kuthana ndi mavuto. Mwinanso kumakhala kuonjezera mavutowo chifukwa kumakhala kosavuta mwamuna kuzunza mkazi amene akumuona kuyi alibenso kolowera.
Popeza mwanena kuyi mukugwira ntchito, langizo langa likhoza kukhala lakuyi, simungagwiritseko gawo lina la ndalama zimene mukulandira polipira sukulu? Mutabwerera kusukulu, ngakhale mukugwira ntchito, zikhoza kuthandiza. Alipotu ambiri amene leto lino akuvhita bwino koma sukulu adaphunzira akugwira pakhomo la munthu.
Chofunika nkuwagoyokozera bwino abwana kapena adona anu kuti sukulu siyikulepheretsani kugwira bwino ntvhito pakhomo lawo. Zabwjno zonse.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Nsanje yakula Anatchereza, Poyamba ndithokoze chifukwa cha kwanu kutithandiza pamavuyo amene timakumana nawo.
Ndili ndi chibwenzi chimene chakhala chikunena kuti chidzandikwatira mu 2017. Koma akangomva kankhani kakangono, amakhumudwa ndipo amathetsa chibwenzi.
Izi zakhala zikuchitika kanayi konse. Nkhani yalero ndi ya pa Facebook, pomwe mnyamata wina wandiyamikira momwe ndikuonekera lachithunzi china.
Bwenzi langayo akuchita nsanje kuganiza kuti ndijuyenda ndi mnyamatayo koma ayi.
Chonsechotu ndidamupatsa password yanga kuti aziona ngakhale mauthenga anga obisika. Zikundisowetsa mtendere nditani.
GK, Mulanje.
GK, Mwamunayo wamukonda, mpaka kumupatsa password! Chikondi chiyenera khbwezeredwa. Kodi iyeyo adakipatsa password yake? Ena amati nsanje ndi maziko a chikondi koma nsanje ina inyanya. Nsanje ina I asonyeza kuti wochita nsanjeyo ndi kamberembere chifukwa amaganiza kuti zimene amachita ndiye kuti enanso akateto zili choncho.
Mwachitsanzo, mwina iye naye amauza asungwana ena kuti zithunzi zawo zikumusangalatsa nchokinga chakuyi awakope tsono akuona ngati mnyamata aliyense akakuuza chimodzimodzi ndiye kuti nayenso akufuna kukukopa. Pomwe si zili choncho.
| 2 |
Papa Wati mu Utatu Woyera Muli Chikondi Chozama cha Mulungu Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco, wati Utatu Woyera wa Mulungu ukuyimira chikondi chozama chomwe Mulungu amakhala nacho pakati pa anthu.
Malinga ndi malipoti a wayilesi ya Vatican, Papa walankhula izi la Mulungu, kulikulu la mpingo-wu ku Vatican, pa tsiku lomwe mpingo umachita chaka cha Utatu Woyera wa Mulungu.
Iye wati chikondi pakati pa Mulungu Atate, Mulungu Mwana komanso Mulungu Mzimu Woyera ndi chikondi chopulumutsa popeza Mulungu adakonda dziko la pansi kotero adatumiza mwana wake Yesu Khristu.
Papa Francisco wati Utatu Woyera wa Mulungu umawulula chikondi cha Mulungu chosasimbika, chikondi chomwe iye wati chili pakati pa eni atatuwo.
Iye wati chikondi cha Mulungu Atate, Mulungu Mwana ndi Mulungu Mzimu Woyera ndi chikondi cha pa mwamba komanso chopulumutsa chifukwa Mulungu adakonda dziko la pansi kotero adatumiza mwana wake Yesu Khristu kudzapulumutsa anthu.
Papa Francisco wati Mulungu amakonda anthu ake, Mulungu amakonda dziko la pansi angakhale kuti dziko la pansi ndi lodzadza ndi uchimo.Iye wati Mulungu amakonda anthu ake posayanganira mphulupulu zawo.
Papa Francisco wati kudzera mchaka cha Utatu Woyera Mulungu amaitana anthu ake kuti afike pafupi ndi kukhala anthu osinthika ndi chikondi chodabwitsa chimenechi cha Utatu Woyera.
Iye wati akhristu amalandira za ulere za Mulungu kudzera mma Sakramenti komanso powerenga ndi kumvetsera Mau a Mulungu. Papa Francisco wati kudzera mma Sakramenti akhristu amakhala mu ubwenzi ndi Utatu Woyera, ubwenzi womwe umabweretsa umodzi ndi mtendere pakati pa anthu.
Pa mwambowo iye wapempherera mwa njira ya padera maiko amene akhudzidwa kwambiri ndi mliri wa Coronavirus.
Pamenepa iye wati kusonkhana kwa anthu pa bwalo la Saint Peters Square patapita pafupi miyez itatu izi zisakuchitika ndi nkhani yosangalatsa kuti mliri wa Coronavirus ndi wotheka kuthetsa komabe iye wachenjeza kuti anthu akuyenera kupitiriza kusamala kutsata ndondomeko zoyikika pofuna kupewa nthendayi.
Pomaliza iye wakumbutsa a Katolika kuti mwezi wa June ndi mwezi wa Mtima Woyerayera wa Ambuye Yesu ndipo wapempha kuti anthu akonde kulemekeza Ambuye Yesu wokhala mu Ukaristia.
| 13 |
Chisankho chipitirirebwalo .Khoti lalikulu likana pempho la MEC Bwalo lalikulu la milandu la Supreme Court Lachinayi lidakana pempho la bungwe la zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) kuti zokonzekera chisankho ziimikidwe kaye mpaka mlandu omwe bungwelo likuchita apilo kuti bwalo la Constitutional Court silidagamule bwino.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mwa zina, woimira MEC Tamando Chokotho adauza oweruza 7 kuti MEC imafuna kuti zokonzekera chisankho ziimikidwe chifukwa bungwelo lidali ndi nthawi yochepa kuti likonzekere. Constitutional Court idalamula pa 3 February kuti chisankho cha pa 21 May 2019 sichidayende bwino ndipo chisankho china chichitike pasanathe masiku 150.
Chakwera ndi Chilima kutuluka kubwalolo chigamulo chitaperekedwa Koma malinga ndi Chikosa Silungwe yemwe ndi woimira wodandaula woyamba mtsogoleri wa UTM Party Saulos Chilima adati majajiwo palibe adaonapo pa mfundo za MEC.
Izi zikutanthauza kuti MEC iyenera kupitiriza zokonzekera chisankho chimene aphungu adati chidzakhalepo pa 19 May chaka chino.
Bwalo la Supreme pa 15 April lidzayamba kumva nkhani imene MEC komanso mtsogoleri wa dziko lino adakamangala kukhoti kuti chigamulo choti sichidayende bwino achitaye.
Padakalipano, MEC yalemba maloya a ku South Africa kuti adzaimire bungwelo ndipo adzawalipira K600 miliyoni. Koma unduna wa zachuma wati sukudziwapo kanthu pankhaniyi imene akadaulo ena ati nkuononga chuma cha boma. Izi zili apo, khumbo la Amalawi ena loti mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika asadikire masiku 21 omwe malamulo amampatsa kuti asayinire mabilu omwe aphungu a Nyumba ya Malamulo avomereza ladzutsa mavu mkhomola.
Mutharika akuyenera kusaina mabilu okhudza momwe chisankho chobwereza cha Pulezidenti chiyendere ndipo pa masiku 21 omwe adali nawo, iye watsala ndi 5 koma malingaliro a Amalawi ena kuphatikizapo HRDC adali oti Mutharika asadikire masiku 21.
Malingalirowo amachokera pa nkhawa yoti chisankho chomwe chikuyenera kuchitika pa 19 May 2020 chikudikira mabiluwo ndiye kuchedwetsa kusainira mabiluwo kukhoza kusokoneza zokonzekera za chisankhocho.
Pofuna kukakamiza Mutharika kusaina mabiluwo msanga, HRDC idalengeza pamsonkhano wa atolankhani pa 6 March 2020 kuti idzatsogolera Amalawi kukatseka nyumba za boma za Kamuzu Palace, Chikoko Bay ndi Mzuzu State Lodge pa 25 March 2020.
Potsatira chikonzerocho, apolisi adamanga atsogoleri atatu a HRDC omwe ndi Timothy Mtambo, Gift Trapence ndi MacDonald Sembereka powaganizira kuti adaphwanya magawo 103, ndi 124 amalamulo adziko lino. Kumangidwako kudadza Mutharika atanena pamsonkhano kuti apolisi ayenera kugwiritsa mphamvu zawo kuti zionetserozo zisachitike.
Gawo 103 la malamulo a polisi limaletsa munthu aliyense kapena gulu kukakumana kufupi ndi nyumba ya chifumu pa mamita ochepera 100 pomwe gawo 124 limaletsa munthu kutuntha anzake kuti aphwanye lamulo zomwe akuluakuluwa achita, idatero kalata yapolisi.
Atatuwo adatulutsidwa pabelo Lachinayi ndipo bwalo lidagamula kuti apereke ndalama yokwana K200 000 ndipo azikaonekera kulikulu la apolisi ku Area 30 ku Lilongwe. Iwo adalangizidwanso kuti asasokoneze zofufuza za mlanduwo ndipo apereke shulite ya K2 miliyoni aliyense.
Msabata ikuthayi, chipani cha Malawi Congress Party (MCP) chidaimitsa kaye zionetsero zimene chidakonza kuchita Lachinayi pofuna kukakamiza apolisi kutulutsa atatuwo.
Koma kadaulo pa zamalamulo Prof Edge Kanyongolo adati pakadalipano, Mutharika sadaphwanye lamulo lililonse posasayina mabiluwo potengera malamulo.
Gawo 73 la malamulo limapereka masiku 21 kwa Pulezidenti kuti asayine bilu ndiye panopo masikuwo sadakwane komanso gawoli limati Pulezidenti ali ndi ufulu wobweza bilu yosasayina koma ndi zifukwa, adatero Kanyongolo.
Iye adapitiriza kuti biluyo ikabwerera ku nyumba ya malamulo ndi zifukwazo, Gawo 73 (4) limapereka mphamvu ku Nyumba ya Malamulo kuunika zifukwazo nkulibwenzanso kwa Pulezidenti kuti asayine.
Zikafika pa ndime iyi, Pulezidenti sakhalanso ndi mwayi wosankha kusayina kapena ayi chifukwa gawoli limati Pulezidentiyo asayine pa masiku 21 basi ndipo akalephera apo, ndiye kuti tsopano waphwanya malamulo, adatero Kanyongolo.
Koma mneneri wa Pulezidenti Mgeme Kalirani adati Mutharika sakuthamangira kusayinira mabiluwo chifukwa malamulo amampatsa masiku 21 ndipo masikuwo sadakwane.
Pazokonzekera za chisankho chobwereza, mneneri wa Malawi Electoral Commission (MEC) Sangwani Mwafulirwa adati bungwelo lidzatulutsa ndondomeko ya zokonzekera zonse zikapsa.
| 11 |
Boma Liyamikira YONECO h="305" height="345" />Anayendera wailesi ya YONECO-Botomani Boma layamikira ntchito yabwino yomwe bungwe komanso wayilesi ya YONECO ikugwira polimbikitsa kupititsa patsogolo mauthenga atsopano ICT komanso kulimbikitsa mapologalamu ambiri othandiza achinyamata ana komanso amayi.
Nduna ya zofalitsa nkhani ndi maluso otumizira mauthenga amakono a Mark Botomani omwenso ndi Phungu wakunyumba yamalamulo wadera la Zomba Chisi ndi yemwe wanena izi lachisanu pambuyo poyendera wayilesi ya YONECO mu mzinda wa Zomba.
Ndunayi yati ndi yokondwa kamba koti luso lopititsa patsogolo mauthenga atsopano kudzera njira zosiyanasiyana zikukonzedwa ndi achinyamata zomwe ati zikufunika kupeza njira zabwino zodzitezera kuti lusoli lisabedwe.
| 14 |
Apempha Akhristu Afikire Osowa mu Nyengo ya Khilisimasi Bambo George Kaliati otumikira mpingo wa katolika mu arkidayosizi ya Blantyre, apempha akhristu a mpingowu mdziko muno kuti afikire anthu osowa mu nyengo ya Khilisimasi yomwe ikudzayi.
Iwo anena izi loweruka ku Limbe Cathedral mu arkidayosizi ya Blantyre pambuyo pa m`bindikiro wa tsiku limodzi wokozekeretsa akhristu a mparishiyi nyengo ya khilisimasi yomwe ikudzayi.
Bambo Kaliati kujambulitsa ndi ena mwa akhristu omwe anali nawo pa mbindikirowo Bambo Kaliati omwe ndi bambo mfumu a parish ya St. Pius mu arkdayosiziyi omwe anatsogolera m`bindikilowu, ati akhristu achikatolika akuyenera kuchita khrisimasi yawo mwachikhiristu mosiyana ndi momwe anthu a mdziko amachitira.
Khirisimasi ya akhristu ndi yosiyana ndi anthu achikunja, ife akhrisitu tikuyenera kukulitsa moyo wauzimu monga kupemphera komanso kulapa, anatero bambo Kaliati.
Khirisimasi ndi nyengo, osati tsiku, anaonjezera motero bambo Kaliati.
Bambo Kaliati anapitiriza kupempha akhristu achikatolika kuti afikire anthu omwe ndi osowa mu nyengo imeneyi ponena kuti nyengoyi ndi yowonetsa chikondi cha Mulungu kwa anthu ake.
Anthu ena akuyenera kuziwa chifundo cha Mulungu mu nyengo imeneyi kudzera mu zitsanzo zathu zabwino, anapitiriza motero bambo Kaliati.
Mau ake wapampando wa tchalitchi la Limbe Cathedral a Andrew Kabvala anati akhristu, m`bindikirowu wawapindulira kwambiri makamaka pakumvetsetsa khrisimasi yomwe ikuphatana kwatunthu ndi kubadwa kwa Yesu Khrisitu.
Tazindikira kufunika kwa kulapa makamaka pamene tikukonzekera kubadwa kwa Yesu Khristu, anatero a Kabvala.
Anthu omwe anatenga nawo gawo pa m`bindikirowu ndi akhristu onse ozungulira tchalitchi la Limbe ndi ena ochokera mmatchalitchi omwe azungulira tchalitchichi. Cholinga cha mbindikirowu chinali kuwakozekeretsa akhristu kubadwa kwa Yesu Khristu komanso zoyenera kuchita mu nyengo ino ya Advent.
| 13 |
Kuwani Wati Alimbikitsa Mgwirizano Wake Ndi Anthu Akumidzi Mtsogoleri wa chipani cha Mbakuwaku Movement for Development (MMD) Peter Driver Sinosi Kuwani wati chipani chake chidzatukula miyoyo ya anthu a mmadera a kumidzi akazasankhidwa ngati mtsogoleri wa dziko lino pa chisankho cha president chomwe chichitike pa 2 July chaka chino.
Kuwani amalankhula izi lachitatu mu mzinda wa Blantyre atamaliza kupereka zikalata zake zowonetsa chidwi chodzapikitsana nawo pa chisankhochi.
Iye anati zipani zomwe anthu amadziona ngati ndi zikulu zikulu mdziko muno zilibe upangiri wabwino ofuna kupititsa patsogolo miyoyo ya anthu a mmadera akumidzi.
Ifetu a Mbakuwaku Movement of Development sitinayambe zandale chifukwa choti tasowa chochita koma tufuna tikonze dziko pophwasula akamberembere, anatero Kuwani.
Ndipo iye wati ichi ndi chifukwa chake chipani cha Mbakuwaku chinakana kulowa mu mgwirizano ndi zipani zina pokonzekera chisankhochi.
| 11 |
Apolisi anjatidwa pokhudzidwa ndi ophedwa pa zionetsero Apolisi asanu ndi anayi adatengedwa msabatayi powaganizira kuti akudziwapo kanthu pa za ena amene adaphedwa pazionetsero za pa 20 Julaye 2012.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Anthu 20 adaphedwa pazionetserozo zomwe Amalawi adachita mmizinda ya Blantyre, lilongwe, Mzuzu ndi Zomba pokwiya ndi ulamuliro wa yemwe anali mtsogoleri wa dziko lino Bingu wa Mutharika. Pofuna kuletsa zionetserozo apolisi adaombera ena mwa iwo.
Wachiwiri kwa mneneri wa kulikulu la polisi Kelvin Maigwa adati apolisi Lachitatu adamanga Sub Inspector Kamwala wa kupolisi ya Lumbadzi, Sergeant Makokezi wa PMF ku Lilongwe, Sergeant Kanyama wa ku Mchinji ndi Constable Lobo wa kupolisi ya Kawale omwe amasungidwa kupolisi ya Lilongwe.
Ndipo malinga ndi mneneri wa polisi mchigawo cha kumwera Nicholas Gondwa, ku Blantyre Paul Mussa, Kelvin Nyirenda, Benedicto Dzombe, Mahomed Kulusinje komanso Lemekezo Mikuti, omwe ndi apolisi ya Ndirande, adatsekeredwa powaganizira kuti akukhudzidwa ndi imfa ya anthu awiri ku Ndirande pa zionetserozo.
Apolisiwo amayembekezeka kukaonekera kukhoti dzulo.
Anthu 20 atafa pazionetserozo, Mutharika adakhazikitsa bungwe lofufuza chomwe chidachitika patsikulo ndipo zotsatira zake zidatuluka muulamuliro wa Joyce Banda, pomwe zidaoneka kuti apolisi adalakwa kuombera anthuwo.
Mabungwe oposa 80 adakonza zionetserozo. Zofuna za Amalawi zidayalidwa mmasamba 15 a chikalata chimene chidatulutsidwa.
Zina mwa zolira za Amalawiwo pazionetserozo zidali kusowa kwa mafuta, ndalama zakunja, kubwera kwa bajeti yosadalira ndalama zakunja, kusowa kwa ufulu wa aphunzitsi msukulu za ukachenjede komanso kuthamangitsa kazembe wa ku Mangalande kuno ku Malawi.
| 7 |
Msonda: Tsamba loyoyoka mu PP? Nthawi yomwe anthu akuchoka mchipani cha Peoples Party (PP) chitangogwa mboma, mneneri wa chipanichi, Ken Msonda, yemwe ali ndi lilime lakuthwa komanso amayankhula mokhadzula, amawayerekeza anzawowo ngati masamba ouma amenene akuyoyoka mmitengo nthawi ya chilimwe.
Lero zagwa pamphuno.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Wachoka mu PP: Msonda Kodi pano Msonda nditsamba louma limene lathothoka mchipani chakale cholamula kuti zichitire ubwino chipanichi? Wogwirizira utsogoleri wa PP, Uladi Mussa akuti Msonda, ngati wina aliyense, ali ndi ufulu wochoka mu chipanichi.
Msonda akunenetsa kuti iye ndi katakwe pandale ndipo kuchoka kwake mchipanichi sikutanthauza kuti ukatakwe wake pandale watha, ayi, koma akumvera zimene Mulungu wake akumuyankhula.
Iye dzana Lachinayi adalonjedza kuti auza mtundu wa Malawi zifukwa zochokera mchipanichi ndi zomwe akulingalira kuchita pamoyo wake mtsogolomu pamsonkhano wa atolankhani mumzinda wa Blantyre, koma dzulo, iye adasintha thabwa ndi kuuza atolankhani kuti msonkhanowu walepheleka atamvera malangizo a mbusa wake.
Abusa anga andiuza kuti ndisapangitse msonkhano wa atolankhaniwu. Akuti ndidekhe kaye mpakana nthawi yoyenerera yokhazikitsidwa ndi Mulungu itakwana.
Ndikupempha anthu kuti andimvetsetse. Monga mmene ndanenera kale, ndikufuna kuzamisa moyo wanga wa uzimu komanso kukhala ndi nthawi yokwanira ndi banja langa, Msonda adatero.
Mkuluyu adati adayankhulana ndi mtsogoleri wa chipani cha PP, Joyce Bandaamene ali kunja kwa dziko lino komwe akhala chigonjereni pazisankho za mu 2014za kuchoka kwake.
Msonda adati Banda adamupempha kuti asachoke msanga kufikira iyo atabwerera ku Malawi, koma idati izi sizikadagwirizana ndi chikonzero chake chopempha Mulungu kuti amutsogolere pa za tsogolo lake mundale komanso muuzimu.
Iye adati zomwe amayankhulira anzake powayerekeza ngati masamba ouma amene akuthothoka mumtengo nthawi ya chilimwe zidali gawo la ntchito yake potumikira chipani.
Ngati mmeneri wa chipani, ndimayenera kuyankhulira chipani komanso kupereka chithunzithunzi chabwino cha chipanichi kumtundu wa Malawi. Koma izi sizikusonyeza kuti ine ndi tsamba louma lomwe latha ntchito.
Poti ndanena kuti ndikufuna ndizame muuzimu kaye, za ine akambe ndi anthu. Ndale ndazisiya kale apo, koma mtsogolomu mundiona ndikuzapanga nawo mpikisano pachisankho cha aphungu a ku Nyumba ya Malamulo mu 2019, Msonda adatero.
Mkuluyu, yemwe wakhala akusintha zipani komaso amadziwika kwambiri ndi dzina loti Foot Soldier, akuti panthawi yoyenera adzauza anthu dongosolo limene akupempha Mulungu kuti amukonzere.
Msonda, yemwe lilime lake lamuikako mmavuto potengeredwa kukhoti atamemeza anthu kuti azipha anthu amene amagonana amuna okhaokha kapena akazi okhaokha, adalowa mu chipani cha PP mu January 2012, chipanichi chisanalowe mboma koma mayi Banda ali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino malemu Bingu Wa Mutharika.
Iye adasankhidwa kukhala mneneri wa PP ndipo udindowu udapitirira chipani cha PP chitalowa mboma potsatira imfa ya Bingu wa Mutharika.
Msonda, yemwe adakhalakonso wothandizira mmeneri mchipani cha UDF asadalowe PP, wakhala akusowetsa mmtendere chipani cholamula ndi kuyankhula kwake kokhadzula, ndipo kumayambiriro a chaka chino, adauzapo mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika kuti atule pansi udindo wake kaamba koti alephera kukonza vuto la zachuma ndi zina.
Izi anayankhula kumsonkhano wa anthu onse okhuzidwa wa Public Affairs Committee (PAC)mu mzinda wa Blantyre, ndipo kuyankhula uku kudakwiyitsa nduna zambiri zomwe zinkatenga nawo gawo kumsonkhanowu.
Chipani cha PP chakhala chikutaya atsogoleri ake ofunikira kwambiri kuphatizapo Sidik Mia, yemwe adatula pansi udindo wake ngati pulezidenti wothandizira mchigawo cha kummwera chisankho za 2014 chitatsala pangono.
| 11 |
Maule akusambabe wamkaka Khomo la ukwati silisowa. Mbanja la Nyasa Big Bullets kudakali chisangalalo kutsatira chipambano chawo pobabata asilikali a ku Mzuzu, Moyale Barracks.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Inde ndi asilikali, koma Loweruka lapitali adalira ndi kukukuta mano atadzidzimutsidwa ndi Bullets yomwe idachita ukali kumapeto kwa masewerowo pamene Moyale imafuna iyambe kusangalala.
Ichotu chidali chikho cha Presidential Cup chomwe wopambana adatenga K10 miliyoni ndipo wogonja kutenga K5 miliyoni.
Moyale idachinya pa mphindi 38 mchigawo choyamba kudzera mwa Wiseman Kamanga. Idalimba poteteza chigolicho mpaka mphindi 90 mchigawo chomaliza.
Ochemerera Bullets kusamba mkaka Goloboyi wa Moyale, Juma Chikwenga ndi osewera onse a Moyale adayamba kupha nthawi apo woimbira Duncan Lengani akuganiza zothetsa masewerowo ikangotha nthawi yoonjezera.
Mpanipani udali ku Bullets ndipo mphunzitsi wawo Franco Ndawa adalowetsa osewera kutsogolo anayi; Chiukepo Msowoya, Diverson Mlozi, Mussa Manyenje ndi Aimable Nikiyiza ndipo Bullets imadza ngati mbandakucha.
Patatha mphindi 93, wosewera wa Moyale adachita thengenenge mpaka kugwira mpira kupezetsa Bullets penote ndipo Msowoya adachinya kuti masewerowo alowe mmapenote.
Pilirani Zonda ndi Msowoya adaphonya mapenote a Bullets pamene Yamikani Fodya, Miracle Gabeya, Nikiyiza ndi Fisher Kondowe adachinya.
Love Jere ndi Chrispine Fukizi a Moyale adagwiritsa mapenote awo ndipo Sandress Munthali, Mtopijo Njewa ndi Timothy Nyirenda adamwetsa. Boy Boy Chima adamenyetsa chitsulo kupangitsa kuti Maule atenge chikhochi.
Ochemerera Bullets adayenda ndi mimba, ena kuvula zovala ndi ena kusamba mkaka kusangalala kuti timu yawo yatenga chikho. Osewera a Moyale adagwa pansi, kulira mosatonthozeka.
Fodya adati loto tsopano lasanduza zochitika, Mulungu adali mbali yathu, zidali zovuta koma Mulungu wazitheketsa, adatero iye.
| 16 |
Papa Wapempha Mabungwe Alimbikitse Nkhani za Chuma Wolemba: Thokozani Chapola p-content/uploads/2019/11/pope-and-ICI.jpg" alt="" width="560" height="314" />Papa ndi mamembala a bungwe la CIC Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisko wapempha mabungwe osiyanasiyana kuti alimbikitse nkhani za chuma zomwe zingathandize pothetsa umphawi.
Papa amalankhula izi pamene anakumana ndi mamembala a bungwe la Council for Inclusive Capitalism (CIC).
Iye wati pamene umphawi ukupitilira kukwera pa dziko lonse, mayiko ambiri akukumananso ndi mavuto monga tsankho komanso kugawikana kwa anthu ndi mayiko, ndipo zikusowa ulamuliro wabwino omwe ungathetse mavutowa.
Papa wakumbutsa mamembala a bungweli kuti munthu aliyense amene akukhudzidwa ndi nkhani za chuma komanso za malonda ali ndi ntchito yotumikira anthu pokweza chuma cha dziko lonse.
Bungwe la Council for Inclusive Capitalism ndi bungwe lomwe silipeza phindu pa ntchito zake ndipo limalimbikitsa umodzi pa nkhani za chuma pa dziko lonse.
| 2 |
Kukweza mafumu kwalowa ndalemafumu Mkwezakweza wa mafumu womwe mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda, wachita chitengereni mpandowu wanyanyula mafumu. Iwo apempha kuti mtsogoleriyu aziona zingapo asanakweza mafumu.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mafumuwa, omwe sadafune kutchulidwa maina awo komanso boma lomwe akuchokera, ati pamiyezi 7 ndi theka yomwe mtsogoleriyu wakhala akulamula, ndi zosamveka kuti angakhale atakweza kale mafumu ochuluka chotere mmipando yawo.
Iwo, omwe akuganiza kuti kukweza kwa mafumuku kumadza pazifukwa za ndale, ati akudabwa kuti mmaboma ena mulibe mfumu yandodo (Senior Chief) koma pokweza mafumu akumakakwezanso mmaboma omwe ma Senior Chief alipo kale.
Mwachitsanzo, mboma la Mwanza muli ma T/A awiri ndi Sub T/A mmodzi ndipo mulibe Senior Chief, yemwenso madera ena amatchedwa kuti mfumu yandodo.
Mboma la Mwanza muli ma T/A anayi koma mulibenso mfumu yandodo.
Mmaboma ena monga Kasungu mfumu zandodo zilipo zinayi, Karonga imodzi, Rumphi imodzi, Chitipa ziwiri, Nsanje ziwiri, Mzimba ziwiri ndi Ntcheu ziwirinso.
Ifenso tikudabwa kuti kodi apulezidentiwa akuyangananji akamakweza mafumu? Nthawi zonse akumati akuyangana ntchito zawo, kodi kanthawi komweka mafumu awakwezawa awawona bwanji? Bwanji mmaboma ena akukhazikitsa atambala awiri pamene ife tilibe tambala? idatero mfumu ina, yomwe idati zotere zichititsa kuti mafumuwa azichita zosangalatsa Pulezidenti ncholinga choti akwezedwe.
Ntchito yathu tikugwira mokayika komanso tikufooka chifukwa sitikudziwa kuti amene awakwezawo akumawayangananji, idatero mfumuyo.
Koma nduna ya maboma aangono, Grace Zinenani Maseko, yati sithirapo ndemanga pa nkhaniyi pokhapokha apeze mafumu omwe akudandaulawo.
Ndiyankhulapo pankhaniyi ndikapeza mafumu omwe akudandaulawo. Sindikutanthauza kuti sindiyankhula koma ndipeze kaye odandaulawo. Sindingakuuzeni tsiku lomwe ndipeze mafumuwa, adatero Maseko.
Bester Mandele, bwanamkubwa wa boma la Rumphi, komwe kwakwezedwa T/A Mwankhunikira kukhala STA, wati iye ngati bwanamkubwa samatengapo gawo pakukwezedwa kwa mafumu.
Timapereka malipoti a momwe mafumu akugwirira ntchito boma lonse koma za mfumu yomwe ikwezedwe ndiye sizitimakhudza, adatero bwanamkubwayo.
Senior Chief Kalonga ya mboma la Karonga yati singayankhire nkhaniyi chifukwa nayonso idakwezedwa.
T/A Chekucheku ya mboma la Neno yati ndi bwino boma lililonse likhale ndi mfumu yandodo koma ikudabwanso kuti kumeneko kulibe mfumu yandodo.
Ufumu wa Chekucheku uli ndi mbiri yabwino monga mmene ulili ufumu wa Kwataine. Takhala tikudikira kuti nafenso tikhale ndi mfumu yaikulu chifukwatu imatithandiza zambiri, idatero mfumuyo.
Senior Chief Kaomba ya mboma la Kasungu yati singaikire ndemanga pankhaniyi koma pakufunika kuti pokweza ufumu pazitsatidwa ndondomeko yake maka mbiri ya mfumuyo.
Kaomba adati ngati zimenezi sizikutsatidwa ndiye kuti kukwezaku kukuchitika mwandale.
Izi zikudza pamene bungwe loona za malamulo la Malawi Law Commission lili mkati kuchititsa misonkhano yokozanso malamulo okhudza mafumu.
Malamulo a dziko lino okhudza ufumu adakonzedwa pa 29 Disembala 1967. Malamulowa amapereka mphamvu kwa mtsogoleri wa dziko, malinga ndi gawo 4 (1), kuti atha kusankha Paramount Chief kapena Senior Chief.
Boma, kudzera mu unduna wa maboma aangono ndilo lidapereka ntchito yokonzanso malamulowa ndipo misonkhano yomva maganizo a anthu yachitika mzigawo zonse zitatu za dziko lino.
Lachinayi pa 27 Sepitembala 2012 msonkhanowu udachitikira ku Hotel Victoria mumzinda wa Blantyre ndipo anthu osiyanasiyana, kuphatikiza mafumu a mmaboma la Zomba, Chiradzulu, Blantyre, Neno, Mwanza, Nsanje ndi maboma ena adasonkhana.
Mfundo yomwe idakula pamsonkhanowo ndi yoti malamulowa akonzedwe kuti mtsogoleri wa dziko asamakweze mfumu pongoloza koma azidutsa kwa abanja komanso bwanamkubwa wa bomalo.
Mafumuwo adati zipani zolamula ndizo zikuwononga mbiri ndi ntchito ya mafumu chifukwa powakweza sakumayangana mbiri ya ufumuwo komanso khalidwe la mfumuyo.
Wapampando wa bungwe lomwe likuchititsa kafukufukuyu, Anaclet Chipeta wati ntchito yomva maganizo a anthu yatha ndipo atumiza lipoti lazomwe apeza kwa nduna ya za chilungamo.
| 8 |
Papa ndi Okhudzidwa ndi imfa ya anthu ku Malawi, Mozambique ndi Zimbabwe Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco wati ndi okhudzidwa ndi imfa ya anthu ochuluka mmaiko a Malawi, Zimbabwe ndi Mozambique amene afa kaamba ka mphepo ya mphanvu yomwe inawomba mmaikowa.
Papa amalankhula izi pa zonkhula-lankhula zomwe amakhala nazo lachitatu lililonse kulikulu la mpingowu ku Vatican.
Iye wati ndi okhuzidwa ndi anthu omwe afa mmaikowa komanso ena omwe akuvutika ndi njala komanso kusowa kwa malo okhala kaamba kavutoli.
Pamenepa Papa Francisko wapempha akhristu mu mpingowu kuti akhale patsogolo kuthandiza anthuwa kudzera mmapemphero komanso zinthu za kuthupi monga chakudya ndi zina.
Mtsogoleri wa mpingo wa katolikayu wapempherera mwapadera anthu omwe akhuzidwa ndi vutoli ndipo wapempherera mizimu ya anthu omwe afa pa ngoziyi kuti iwuse ndi mtendere wosatha.
| 14 |
Pezani umuna wa ngombe Nthawi yokhala ndi ngombe za makolo yapita. Ndi K1 500 yokha, alimi akhoza kupeza umuna wa ngombe za makono.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Zonse zikutheka kusukulu ya zaulimi ya Mikolongwe komwe kukupezeka mbewu za ngombe zamkaka za Friesian Holstein. Ndiye palinso mtundu wa nyama ya ngombe zamkaka za Brahman zomwe ndi za mtundu wa nyama ndi mtundu wa Jersey zomwenso ndi za nyama komanso mkaka zimatulutsa wambiri. Malinga ndi yemwe amayanganira nthambi yosunga umuna wa ngombe kusukuluyo, Innocent Mboma, njira yogula umuna ndi yachidule, yosamala komanso yotchipa ndipo alimi akuyenera kutsatira njirayi ngati akufuna mitundu ina ya ngombe.
James Molende kukolola umuna kwa ngombe ya mtundu wa Friesian Madera ambiri kuti ugule ngombe ya mphongo, mtengo wotsikitsitsa ndi K150 000 ngombe imodzi mtengo woti mlimi sangakwanitse.
Nchifukwa chake tikugulitsa umuna kuti alimi asavutike. Umuna wa K1 500 wokha angathe kukakweretsa ngombe imodzi ndipo ndi kamodzi kokha ngombe yatenga bele, adatero a Mboma. Iwo adati umunawu ungakweretsedwe kwa ngombe ya mtundu ulionse ndipo mwana amene akabadweyo akakhala wa mtundu wa umuna omwe adagula.
Kaya ngombe yake ndi ya mtundu wanji, umuna umenewu ukagwirabe ntchito. Ndipo mwana wobadwayo adzatenga bambo ake.
Iye adati umuna umatengedwa Lolemba ndi Lachinayi sabata iliyonse ndipo alimi angathe kupita kusukuluyo tsiku lililonse ndipo umunawo akaupeza.
Pobwera akuyenera kutenga potengera monga fulasiki kuti umunawo usafe. Komanso si kuti alimiwa timangowagulitsa, timawaphunzitsa momwe angasungire komanso momwe angakweretsere ngombe yawo, adatero a Mboma.
Iwo adati patsiku amakolola umuna wochuluka ndi mamililita 10 kwa ngombe imodzi ndipo akaugawa angathe kukweretsa ngombe zazikazi pafupifupi 100.
| 4 |
Limbani Simenti: Kukangalika pa zoimba Ku Malawi kuno kuli oimba zauzimu ochuluka. Mmodzi mwa iwo ndi Limbani Simenti yemwe akudziwika bwino. Iyetu amadziwika kwambiri ndi nyimbo ya Ndikuoneni. CHIMWEMWE SEFASI adamupeza mnyamata wa ku Ndirandeyu ndipo adacheza naye motere: Ndikudziwe.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Pa Wenela pasintha zedi Dzina langa ndine Limbani Simenti, ndimachokera chigawo cha kumwera, mboma la Thyolo, T/A Nsabwe, mmudzi wa Matekenya.
Adaimba Ndikuoneni Baba: Simenti Kodi zoimbaimbazi mudayamba liti? Inetu zoimbaimba ndidayamba pa kanthawi, pamene ndidali sitandade 4, koma chidwi chidayamba kundipeza pomwe ndidayamba kuimba kwaya ya Mount Sinai mu 1999. Mu 2010 pomwe ndidayamba kuimba mu Praise Team ya mpingo wa All for Jesus. Mu 2011 mpomwe ndidatulutsa chimbale changa cha Lungisani Mpiro kutanthauza kuti konzani moyo wanga.
Kodi nkhani zamaimbidwe umaziona bwanji pa Malawi pano? Nkhani za maimbidwe zili bwino pa Malawi. Kungoti ubwino weniweni umaoneka munthu ukakhala ndi chidwi komanso ukaikapo mtima wako wonse, ndi kudziwa chomwe ukufuna pamoyo wako chifukwa zomwe umabzala ndi zomwe umakolola.
Kodi nyimbo yako ya Ndikuoneni imatiphunzitsanji? Ndikuoneni Baba ndi nyimbo yomwe mumapezeka mphamvu. Iyi ndi nyimbo yomwe imatifupikiritsa chifupi ndi Mulungu. Mwachitsanzo, ndikamati Baba ndifuna ndikuoneni imakhala ikusonyeza ife tili paubale weniweni ndi Mulungu, ndi nyimbo yomwe ine uthenga ndimati ndikaumva ndimaona kuti Mlengi ndi amene adandipatsa uthengawo kuti ndilakhule kudzera mnyimbo posonyeza kuti nkhawa zathu timatula kwa Yehova ndi kuonetsa ubale weniweni ndi Mulungu. Nyimbo imeneyi imapezeka mchimbale chotchedwa Lungisani Mpiro chomwe mudali nyimbo 12 monga Uligwindi, Njoka Yokalamba, Yesu Salemphera ndi zina, pamene DVD idatuluka ndi dzina loti Ndikuoneni.
Kodi chaka chino Amalawi ayembekezere zotani kuchoka kwa iwe? Ndikuwalonjeza Amalawi kuti tisanafike kumapeto a chaka chino cha 2015 ndiwapatsira chimbale chomwe chili ndi nyimbo 12, zomwe panopa ndamaliza kujambula.
| 0 |
Aphungu apite mmidzi Pomwe sipikala wa nyumba ya malamulo, Henry Chimunthu Banda walengeza Lachitatu msabatayi kuti aphungu ayamba kukumana pa 18 Meyi, T/A Mwakaboko ya mboma la Karonga yati aphunguwa akuyenera apite kumudzi kukamva zomwe anthu awo akufuna kuti akakambirane.
Mfumuyi yati aphunguwa amangonama kuti zomwe akukambiranazo zikuchoka kwa anthu omwe adawasankha chikhalirecho samapitako.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Mwakaboko wati aphungu akumakhala mtauni zomwe zikulepheretsa kuti mbalizi zizikambirana zosowekera za dera lawo.
Mfumuyi yati ikhala yokondwa kuti pakhale yankho la mavuto a kusowa kwa mafuta agalimoto.
Mwakaboko watinso njira yosankhira ophunzira opita kusukulu ya ukachenjede ikuyeneranso kukambidwa.
Mukumbuka bwino kuti kuno takhala tikudandaula ndi ndondomokoyi ndiye ndibwino aphunguwo akakambirane zimenezi, adatero Mwakaboko.
William Joseph wa mmudzi mwa Goveya kwa T/A Makwangwala ku Ntcheu wati pa 18 pasadafike aphunguwa apite kumudzi kukafunsa osati kumangowaimbira lamya pazomwe akakambirane.
Mlimi wa chimangayu wati ndibwinonso kuti aphunguwa akakambirane zochotsa ndondomeko yosadalira chithandizo chakunja ya Zero-deficit.
Iye wati anthu avutika kwambiri maka pokwera misonkho kwa zinthu chifukwa cha ndondomekoyo.
| 11 |
Kugawana ulamuliro kungatheke ku MW? Pomwe mtsutso ukupitirira pa maganizo woti atsogoleri a dziko lino azigawana zigawo zozilamulira watenga malo, nduna ya zofalitsa nkhani Kondwani Nankhumwa yati gwero la mtsutsowu si zotsatira za chisankho cha pa 20 May kapena momwe mtsogoleri wa dziko lino adasankhira nduna zake.
Pachisankho cha pa 20 May, mtsogoleri wa chipani cha DPP Peter Mutharika adapeza mavoti 36 mwa 100 alionse, kusonyeza kuti anthu 64 mwa 100 alionse samamufuna. Ndipo posankha nduna, Mutharika adasankha nduna 13 zakumwera, zitatu za pakati ndi zinayi za kumpoto. Izi zachititsa ena kunena kuti ndibwino atsogoleri azilamulira zigawo zawo.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Nankhumwa yemwenso ndi woyanganira zisankho ku DPP adavomera kuti nduna zambiri ndizochokera mchigawo cha kumwera koma adati izi zili choncho chifukwa chipani cholamula chidapeza aphungu ambiri mchigawochi kusiyana ndi zigawo zina.
Palibe chachilendo apa chifukwa ndi momwe zimakhalira. Mtsogoleri amasankha nduna kuchokera pa aphungu omwe ali nawo ndiye zidachitika kuti mtsogoleri wa dziko lino adali ndi maina ambiri a aphungu a kumwera. Izi sizingadzetse maganizo ogawana ulamuliro, adatero Nankhumwa.
Nankhumwa adatinso palibe chifukwa chowerengera kuchuluka kwa anthu omwe adasankha chipani cha DPP pachisankho cha pa 20 May 2014 chifukwa zonse zimayendera mmalamulo.
Malamulo achisankho amati yemwe wapeza mavoti ambiri ndiye wapambana ndipo ndiye mtsogoleri ndiye sindikuonapo nkhani powerengera kuti adavota ndi anthu angati kuti ena azinena kuti chigawo chakuti sichimamufuna ndipo akufuna azikhala ndi atsogoleri awo, adatero Nankhumwa.
Magulu ena kudzanso zipani za ndale akhala akupempha kuti zigawo za mdziko muno zikhale ndi utsogoleri wawo kuti chitukuko ndi ntchito zina ziziyenda mofanana.
Ena akhala akudandaula kuti zigawo zina makamaka cha kumpoto sichikutukuka mofanana ndi zigawo zinzake ngakhale kuti zonse zili pansi paulamuliro umodzi.
Mphunzitsi wa zandale kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, Blessings Chinsinga adati omwe akulimbikitsa izi sakuphwanya lamulo lililonse koma akugwiritsa ntchito ufulu omwe ali nawo.
Iye adati mboma la demokalase anthu amakhala ndi mphamvu zosankha mmene akufunira kuti zinthu ziziyendera koma adati izi zimayenera kutsata ndondomeko yomva maganizo a anthu podzera muvoti ya liferendamu.
Kuteroko nkukhwima maganizo pandale chifukwa anthu akusonyeza kuti akuzindikira ufulu wawo koma chofunika nkutsata ndondomeko yoyenerera ya liferendamu, adatero Chinsinga.
Mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika Lolemba adati Amalawi ayenera kukambirana za nkhaniyi kuti mutu wake uoneke.
Nchovomerezeka kupereka maganizo pankhani zosiyanasiyana bola ngati maganizowo akuperekedwa mchoonadi komanso motsata malamulo, adatero Mutharika.
Bungwe lounikira za momwe zinthu zikuyendera mdziko muno la Public Affairs Committee (PAC) lidati zomwe adanena mtsogoleri wa dziko lino ndi mawu a chirimbikitso.
Mneneri wa bungweli bambo Peter Mulomole adati chibukireni nkhaniyi, bungwe lawo lakhala likumenyerera zakuti anthu apatsidwe mpata wopereka maganizo awo.
Iye adati nzosangalatsa kuti atsogoleri aonetsa chidwi chopereka mpatawu zomwe adati zithandiza kuti manongonongo onse okhudza nkhaniyi athe kudzera muchisankho chomva maganizo a anthu.
Ife ngati a PAC tilibe mbali koma cholinga chathu nchakuti anthu apatsidwe mpata wogwiritsa ntchito ufulu omwe ali nawo. Kaya anthuwo adzasankha kusintha kayendetsedwe ka dziko kaya ayi, ife tilibe nazo ntchito koma ziyendere maganizo awo, adatero Mulomole.
Chinsinga adati ngakhale izi zili choncho pakufunika kufatsa bwino chifukwa kuteroko kukhozanso kubweretsa chisokonezo china.
Pakadalipano anthu ambiri sakudziwabe tanthauzo la federalism kapena chitaganya ndipo nkofunika kuwaphunzitsa kaye mokwanira kuti amvetsetse apo ayi tikhoza kudzaonanso mavuto ena, adatero Chinsinga.
Iye adatinso nkofunika kuunikira anthu kuti uwu si mpikisano wa ndale poopa kuti zotsatira za maganizo a anthuzo zingadzatanthauziridwe molakwika potengera kuti ena mwa omwe akulimbikira nkhaniyi ndi azipani za ndale.
Nkhaniyi itangoyamba kumene, mafumu akuluakulu mchigawo cha kumpoto adasonyeza kusagwirizanayo koma adauza nyuzipepala ya The Nation Lolemba kuti ali pambuyo pa maganizowa.
Ena mwa mafumuwa monga Chikulamayembe wa ku Rumphi ndi Kyungu wa ku Karonga adati adatsutsana ndi maganizowa poyamba chifukwa sadafunsidwe ndi omwe amalimbikitsa za nkhaniyi koma pano adafunsidwa ndipo ayimvetsetsa.
| 11 |
Anatchereza Wokondedwa Anatchereza, Zikomo chifukwa cha malangizo amene mukumapereka. Thandizeni.
Ndili ndi mkazi yemwe ndakhala naye kwa nthawi ndithu. Iye adapezeka wodwala ndipo mthunzi wake utatsala miyezi iwiri kuti akhale ndi mwana, makolo ake adamuitanitsa. Pozindikira kuti izi zimachitika, ndidaloleza kuti apite.
Ndipo sindidafowoke kumuthandiza nthawi yonseyo mpaka kuchira. Koma atachira, achibalewo adati ndichoke kumene ndikukhala ndipite kwawoko.
Sindidagwirizane nazo ndipo ndidakana. Mwanayo atabadwa, adati ndisapite kukamutenga koma ndipite komweko tizikakhala. Sindidagwirizane nazo ndipo ndidaneneratu kuti sindingapiteko.
Lero patha miyezi 13, ndipo makolowo akunena kuti ndipite kumudziko ndikamutenge mwanayo. Ndichitenji? SL, Balaka SL, Zikomo chifukwa chondikhulupirira. Choyamba mukuyenera kuzindikira kuti pena anthu amakhala ndi zikhulupiriro zosiyanasiyana. Ndikulangizani molingana ndi kuti simunatiuze ngati mkazi wanu ndi inu muli a mitundu yofanana.
Ngati muli a mtundu umodzi, mukudziwa chimene ndikunena. Komanso mukuyenera kudziwa chimene makolowo akuchitira izi.
Nchifukwa chake ndinganene kuti ngati muli a mtundu umodzi, mwina mukhoza kudziwa kuti panali china chimene amafuna achite naye mwanayo, ndiye amakumangani. Koma chifukwa sizinatheke, nchifukwa akukuuzani mupite.
Koma zonsezo ndi inu ndi mkazi wanu. Kodi maganizo ake ali pati? Akudziwa, akuuzani.
Sindikhulupirira zaufiti, koma izitu ziliko.
Tsono pa ganizo lakuti mukamutenge mwanayo kapena ayi, ndikuuzani motere: mwanayo mukamutenge, chifukwa ndi wanu. Koma mupite kukamutenga patapita nthawi mpaka kutamvetsetsa chimene chikuchitika. Pitirizani kumuthandiza kuti musamuphere ufulu.
Cholinga choti pathe nthawi kaye nchakuti, muone momwe zikukhalira. Panopa, tumizani zofunika.
Anatchereza.
Kodi akazi amafuna chiyani? Zikomo Anatchereza, Ine ndi mnyamata wa zaka 24 ndipo ndikusaka msungwana wakuti ndimange naye banja. Komatu zikundivuta.
Vuto lalikulu ndilakuti sindikudziwa kuti akaziwa amafuna chiyani kwenikweni.
Izitu ndikunena chifukwa cha zomwe ndakhala ndikuziona. Panopa ndafunsira akazi okwana atatu koma chomwe ndikuchiona nchakuti ngakhale akundikana, pakatha masiku angapo, amandiimbira, kapena kuchita zina, kundikopa kuti chibwenzi chiyambepo.
Nchifukwa chiyani akuchita izi? Ndikufuna kukwatira, koma sindikudziwa kuti kwenikweni amafuna chiyani? Thandizeni gogo.
CGS, Karonga CGS, Zikomo chifukwa cha uthenga wanu.
Mkazi asanalole mwamuna ukwati, amadikira kaye ngatidi mwamunayo watsimikiza.
Akatero, amaona kaye ngati mwamunayo angamuthandize. Apa amaunikiranso ngati angayanjane magazi polingalira mtundu, chipembedzo, maphunziro ndi zina zotero.
Malingaliro otero angabweee patatha nthawi tsono nchifukwa chake kuyambira kale amanena kuti ndikuyankha mawa.
Iyi imakhala nthawi yoti akufufuzeni ngati simukudziwana bwino.
Kodi inuyo mbiri yanu njotani? Mwinatu akaziwo sakukudziwani ndiye akafufuza akupeza kuti mulibe banga, nchifukwa chake akubwerera kuti mukwatirane nawo.
Malangizo anga ndi akuyi, musanafunsire, muzimulola mkaziyo akudziweni. Muzimupatsa nthawi yokwanira ndi kumulola kuti akudziweni bwinobwino.
Kupanda kutero, palibe chotheka.
Anatchereza.
| 12 |
Anatchezera Nditani Anatchereza? Agogo, Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Ndine mtsikana wa zaka 20 ndipo ndili ku koleji. Ndili ndi chibwenzi chomwe tidagwirizana kuti tidzamange banja mtsogolo muno. Mnzangayu amati akufuna kuti adzandidziwire mbanja chifukwa akayamba kundigona panopa atha nane filimu. Ndiye akuti poti iyeyu ndi munthu pena zimavuta ndiye akuti akufuna apeze mkazi woti azigonana naye popewa kugonana ndi ine kuti inyeyo adzandikwatire. Kodi kumeneku ndi kukonda? Ndithandizeni, agogo, nditani.
Ndi L, Likuni, Lilongwe Wokondeka L, Funso lako ndalimva ndipo ndikuti wafunsa bwino zedi. Bwenzi lakolo ndi munthu wachilungamo, koma chilungamo chake chaonjeza. Munthu wotere osamukhulupirira chifukwa ndi kamberembere. Iyeyu wanena chinthu chanzeru kwambiri kuti pakalipano musamagonane chofukwa akuopa kuti akatero atha nawe chilakolako chifukwa wakudziwa. Koma akuti akufuna apeze mkazi wina wapambali kuti azikapumirako poti iye ndi munthu, nanga iwe wakuuza kuti nawe utha kupeza wina woti uzicheza naye pamene mukudikira kuti mudzakwatirane? Akunama ameneyo; akufuna kuti azioneka ngati munthu wokhulupirika pomwe ndi wachimasomaso ndi akazi ena. Tikamati kudzisunga ndi nonse awiri, osati wina aziti mnzangawe udzisunge koma ine ndikayendayenda. Kunjaku kwaopsatu, ndiye wina azipanga dala zachibwana ngati zimene akunenazo, si zoona ayi. Ngati ndi wachilungamo, iyenso ayenera kupirira kuchilakolako cha thupi kufikira tsiku lomwe mudzalowe mbanja. Koma ngati adayamba kale zogonana ndi akazi ena, mchitidwe umenewo sadzausiya. Ndiye, kunena zoona, mwamunayo sali woyenerera kumanga naye banja chifukwa alibe chikondi chenicheni ndi iwe. Amati mbuzi ikalawa mchere sigwirika! Amandikakamiza Agogo, Ndine mtsikana wa zaka 16 ndipo ndili ndi bwenzi langa wa zaka 19. Iyeyu amandikakamiza kugonana naye. Ine zimenezo sindimafuna koma ndimalola kupanga naye zimenezo chifukwa ndimamukonda kwambiri ndipo kukana ndimaopa kumukhumudwitsa. Ndiyeno ndipange chiyani kuti mchitidwewu uthe? Zikomo.
| 12 |
Zakudya za ziweto zasowa Mboma la Nsanje, ziweto monga ngombe, nkhosa ndi mbuzi zili pamoto chifukwa cha kusowa kwa chakudya.
Kwauma, ndipo tchire anthu atentha. Nthawi ngati imeneyi zaka zonse, ziweto akuti zimadalira kumtsinje wa Ruo komwe zimakadya bango, nsenjere ndi udzu wauwisi.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Koma chaka chino chifukwa cha madzi osefukira, Ruo wabweretsa mchenga wambiri zomwe zachititsa kuti bango ndi udzu wauwisi ukwiririke. Mulibemo msipu ulionse.
Malinga ndi gulupu Manyowa, ziwetozi zikudalira makoko a chimanga, nthochi kapena zikonyo mwinanso mango.
Ziweto zambiri zikumasonkhana pansi pa mitengo ya mango kuti anthu akamathyola zidyeko. Chifukwa cha kusowa chakudya, ziweto zambiri zaonda, adatero Manyowa.
Koma alangizi amalangiza kuti zikatere alimi amayenera kuti azikhaliratu atapanga zakudya za ngombe ndi mbuzi kuti azizipatsa nthawi ngati ino.
Manyowa akuti mmudzi mwake palibe munthu amene adapanga zakudyazo chifukwa cha mavuto a madzi amene adakumana nawo.
Palibe amene adapanga zakudya za ziweto. Kodi mmene zidalili kuno ungamupeze munthu akupanga zakudya za ziweto? Mlimi aliyense adali ndi chiyembekezo kuti ziweto zizikadyera kumadzi monga zikhalira nthawi zonse osadziwa kuti kukhala mchenga wotere, adaonjeza.
Mneneri mu unduna wa zamalimidwe, Hamilton Chimala, akuti alimi akuyenera kumakhala okonzeka ngati akufuna ziweto zawo zipulumuke nyengo ngati ino.
| 4 |
Manja mkhosi ndi kupsa kwa misika Pamene nkhani yakupsa kwa misika yayala nthenje mdziko muno, amalonda ena achita jenkha, kusowa mtengo wogwira katundu wawo atasakazidwa ndi moto.
Chisale watuluka nkumangidwanso Escom in free-for-all fuel scam Wait gets longer Posakhalitsapa, misika ya Area 18 ku Lilongwe, wa Kasungu, Vigwagwa ku Mzuzu, Kamuzu Road ku Salima komanso wa Karonga yapsa ndipo katundu wa nkhaninkhani wasakazidwa.
Mmodzi mwa okhudzidwa ndi kuyaka kwa msika wa Vigwagwa wati akusowa mtengo wogwira pamene katundu wake wa K1.3 miliyoni adayakiratu.
Kupsa kwa misika ndiyo nkhani ili mkamwamkamwa Ndithandiza bwanji abale anga 11 omwe amadalira ine? Chopweteka kwambiri nchakuti ndidali nditangotenga ndalama kumene kukagula katunduyo, adatero Banda.
Wapampando wa komiti ya pamsika wa Vigwagwa, Gerald Maulana, adati komiti yoona za ngozi za moto yapangidwa yomwe iziona za momwe angathanirane ndi ngozizo komanso kupezeka kwa madzi ozimitsira moto azikhala pafupi.
Maulana adati anthu omwe adali ndi ngongole akuwathandiza powalembera makalata opita kukhonsolo ndi mabungwe opereka ngongole ngati umboni kuti katundu wawo adapsa.
Iye adati: Zaka za mmbuyozo anthu ankagwiritsa ntchito moto ngati njira yobela katundu koma apolisi adakhwimitsa chitetezo ndipo palibe amene adadandaula kubedwa kwa katundu pa nthawi ya moto.
Ndipo Lachitatu polankhula phungu wa pakati mboma la Kasungu Amon Nkhata atapereka simenti yokwana K1.5 miliyoni yogulira matumba 200 a simenti kuti msika wa Kasungu umangidwenso, wapampando wa mavenda mumsikawo Burnet Saudi adati padakalipano manja awo ali mkhosi.
Tikupempha akufuna kwabwino ena athandize mnjira zosiyanasiyana chifukwa mavuto ndiye ngambiri, adatero iye.
Padakalipano, mneneri wapolisi mdziko muno Rhoda Manjolo wati apolisi amayamba afufuza kaye asanamange munthu. Mawuwa adadza pamene mneneri wa unduna wa maboma aangono Muhlabase Mughogho adati kusamangidwa kwa anthu ootcha misika ndiko kukuchititsa mchitidwewu kuti ukule.
Mughogho adati palibe chasintha pa mfundo za chikalata chimene undunawo udatulutsa chaka chatha.
Malinga ndi chikalata cha chaka chathacho, makhonsolo ayenera kukhala ndi zozimira moto zokwanira mmisika kuti ngozi itagwa asasowe mtengo wogwira.
| 15 |
Osolola ndalama za Edzi mitima ili phaphapha! Unduna wa zaumoyo wati zotsatira zakafukufuku wokhudza kusokonekera kwa ndalama zothandizira kulimbana ndi matenda a Edzi zatuluka, koma undunawu ukudikira ndemanga za nthambi yoona zakapewedwe ka matenda ya Centre for Disease Control (CDC) kuti unene tchutchutchu wake.
Pa Wenela pasintha zedi ANatchereza Tidakumana ku sukulu ku Chiradzulu Mlembi wamkulu mu undunawu, Macphail Magwira, watsimikiza za nkhaniyi ndipo wati zotsatirazi azitulutsa mtsogolo muno nkuwona kuti undunawu ungachitenji ndi anthu omwe akukhudzidwa ndi kusokonekera kwa ndalamazi.
Zotsatira za kafukufuku zatulukadi koma zili mmanja mwa nthambi yoona zakapewedwe ka matenda osiyanasiyana kuti nawo aikepo ndemanga zawo. Zikachoka kumeneko, mpomwe tione kuti tingatani potengera zotsatira ndi ndemangazo, adatero Magwira.
Iye adati pa anthu oganiziridwa onse, omwe adzapezeke olakwa adzaimitsidwa ntchito chifukwa chosokoneza ndalama za boma.
Kumapeto kwa chaka chatha, unduna wa zaumoyo udaimitsa ntchito anthu 63 zitadziwika kuti ndalama zina zomwe zimayenera kugwira ntchito yolimbana ndi matenda a Edzi zasokonekera ndipo undunawu umafuna nthawi ndi mpata wofufuzira.
Tidaimitsa anthu ena omwe amaganiziridwa nawo. Ena mwa anthuwa amagwira kunthambi yowerengera ndalama za undunawu, makalaliki ndi ogwira ntchito mmaofesi ena kuti tifufufuze bwinobwino popanda zopinga, adatero Magwira.
Anthuwa adapatsidwa mpaka pa 31 March chaka chino ngati tsiku lomwe angadzayambe ntchito koma mpaka pano anthuwa sadayambebe ntchito kudikira kuti zotsatira za kafukufukuyo zituluke.
Maunduna ndi nthambi zina za boma zakhala zikukhudzidwa ndi kusokonekera kwa ndalama za boma zomwe ena amangoti Kashigeti pofanizira ndi kubedwa kwa ndalama zankhaninkhani kulikulu la boma.
| 7 |
Nthambi za Boma Zikulephera Kulipira Mabilu a Madzi Wolemba: Thokozani Chapola mw/wp-content/uploads/2019/09/nankhumwa.jpg" alt="" width="368" height="326" />Unduna wake ulowelerapo-Nankhumwa Nduna yoona za ulimi mthilira ndi chitukuko cha madzi a Kondwani nankhumwa lachisanu lapitali ati nthambi komanso maofesi ambiri a boma akuti akulephera kupereka ngongole zawo zamadzi ku bungwe la Southern Region Water Board (SRWB).
A NANKHUMWA anena izi paulendo wao oyendera ntchito za bungwe-li pomwe anakayendera malo angapo omwe bungwe-li likugwira ntchito zake monga ku malo a dam la mlunguzi, ndi ena mu mu mzinda wa ZOMBA.
Iwo ati kusaperekedwa kwa mabilu-wa ndi amodzi mwa mavuto omwe mabungwe opereka madzi akukomana nawo mdziko muno, ndipo ati boma liyesetsa kuchitapo kanthu ndi cholinga choti ntchito za bungweli zipite patsogolo.
nkhani zimenezi zikulepheretsa mabungwe opereka madzi mdziko muno kuti agwire ntchito yawo moyenera ndipo ife ngati boma tichitapo kanthu kuti nthambi za boma zomwe zili ndi ngongole ku mabungwe onse opereka madzi mdziko muno abweza ngongolezo, anatero a Nankhumwa.
Malipoti akusonyeza kuti bungwe la Southern Region Water Board lili ndi ngongole zokwana 12.5 billion kwacha zomwe likuyenera kutolera ku nthambi zosiyanasiyana za boma.
| 2 |
Chipembedzo chikukolezera kupemphapempha mmisewu Kukhulupirira chipembedzo kukukolezera mchitidwe wopemphapempha mmisewu, zimene zachititsa kuti ntchito yochotsa opemphawa ivute, watero mkulu wa bungwe limene limachotsa ana mmisewu la Chisomo Childrens Club.
Ngakhale boma lakhala likulengeza kuti aliyense wopezeka akupemphetsa mmisewu adzamangidwa, izi sizikutheka. Sabata zingapo zapitazo, bomalo limalengeza mozungulira mzinda wa Blantyre kuti aliyense wopezeka akupereka ndalama kwa opemphetsa adzamangidwa.
Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Masankhidwe a nduna autsa mapiri pa chigwa Malonjezo ayamba kuoneka Akuti mawu a Mulungu amavomereza kupereka kwa opempha Koma mkulu wa bungweli Auspicious Ndamuwa wati ganizo lochotsa opemphetsa mmisewu silingakwaniritsidwe chifukwa zipembedzo zambiri zimalimbikitsa kupereka. Iye adati chikhulupiriro chopereka chidayala nthenje pakati pa Akhristu ndi Asilamu.
Opemphetsawo amadziwa kuti akapita mmisewu, akakumana ndi anthu opemphera ndiponso a chisoni omwe akawapatse ndalama. Ana ena tikawatenga timawapatsa zofunikira pamoyo wawo, koma ena okonda ndalama ndi kudana ndi sukulu amathawa nkubwerera mmisewu. Akanakhala kuti anthu sapereka ndalama, vutoli bwenzi litatha, adatero Ndamuwa.
Akhristu akuganiziridwa kukolezera mchitidwewu pofuna kukwaniritsa mawu a pa Machitidwe a Atumwi 20:35 omwe akuti: Mzinthu zonse ndakuonetsani kuti mwakugwira ntchito molimbika chomwechi, muthandize ofookawo, ndipo muzikumbukira mawu a Ambuye Yesu. Pajatu iye anati, Kupatsa kumabweretsa chimwemwe chochuluka kuposa kulandira.
Ndamuwa adati Asilamu akutichita izi chifukwa cha Zakati yomwe ndi imodzi mwa ngodya za chipembedzo chawo yomwe achuma amatenga phindu lomwe apeza ndi kugawirako osowa.
Koma mlembi wa Blantyre City Presbytery yomwe ndi gawo la Sinodi ya Blantyre mbusa Baxton Maulidi adati mpingo umathandiza osowa osati kulimbikitsa mchitidwewu chifukwa nthawi ya Yesu opemphetsa adaliponso.
Iye adati vuto ndi kusathandiza anthuwa mokwanira powapatsa njira zoyenera za kapezedwe ka chuma.
Kulumala, ulesi ndi umphawi zimachititsa anthu kupita pamsewu. Koma palinso olumala ochuluka omwe akugwira ntchito ndi kumathandiza alungalunga.
Akhristu sangasiye kuthandiza ena. Chofunika ndi kupeza njira zokhazikika zoti azidalira osati kupempha. Munthu wopemphetsa yemwe Petulo mBaibulo adamuchiritsa sadabwerere pamsewu chifukwa adamuthandiza moyenera, adatero Maulidi.
Ndipo Sheik Alli Makalani wa pa mzikiti wa pa Mangochi pa boma adati Zakati siyikukhudzana ndi anthu opemphetsa chifukwa Chisilamu chimalimbikitsa kugwira ntchito komanso kholo kusamalira ana ake.
Wololedwa kupempha ndi mwana wamasiye yemwe alibe womuthandiza ndi wolumala woti sangagwire ntchito. Koma thandizo lake siliyenera kupempha kumsewu. Amatengedwa ndi kukasamalilidwa kumalo oyenera. Sitikondwera ndi opemphetsa mwadala, iye adatero.
Maulidi ndi Makalani adapempha mabungwe, azipembedzo ndi boma kuti apeze njira zokhazikika zothandiza osowa.
Mneneri wa nthambi ya zosamalira anthu Lucy Bandazi adagwirizana ndi pempholo, koma adati ambiri kupemphetsa ndi khalidwe chabe chifukwa adapindula mundondomeko za boma zowathandiza kuima paokha.
Pali njira ya mthandizi, feteleza wotsika mtengo ndi zina mmatumba a chitukuko. Undunawu umapereka ukadaulo wa ntchito za manja kwa omwe ali ndi ulumali kudzera ku Malawi Council for the Handicapped (Macoha) ndi Mulanje School for the Blind komwe amaphunzira kusoka, kuluka, ukalipentala ndi ulimi. Akamaliza amapatsidwa zipangizo zoyambira moti ambiri akupemphetsa mmisewu adapindula mu ndondomekozi, iye adatero.
Bandazi adati aliyense opereka ndalama kwa opemphetsawa akuthandizira kuphwanya lamulo.
Mavuto omwe amawapititsa mmisewu sangathe ndi kupemphetsa. Ndondomeko za boma ndi zofuna kuti apeze zochita zokhazikika zomwe zipaso zake sizingaoneke nthawi yochepa. Ndi udindo wa aliyense kuonetsetsa kuti anthu osowa akukhala umoyo wabwino, osati mmsewu, adatero Bandazi.
| 13 |
Aphunzitsi adzawalabadire ndani? Ambiri timadzudzula kujombajomba komanso kusalimbikira ntchito kwa aphunzitsi msukulu za boma.
Mchitidwewu ngopititsa pansi maphunziro chifukwa ophunzira amachoka kusukulu asanasulidwe moyenerera.
Chisale watuluka nkumangidwanso Sipakala waimitsa Nyumba ya Malamulo Chakwera akwanitse malonjezoHRDC Koma ambirife tikadakhala aphunzitsi bwenzi tikuchita zofanana kapena zoonjezanso kuponsa mmene ena achitira lero lino, maka tikaona mmene boma limachitira ndi aphunzitsi pa nkhani ya malipiro.
Choyamba, aphunzitsi ambiri amalandira ndalama yochepa kwambiri yomwe njovuta kufikira zofuna za munthu pamoyo wake, choncho nzomveka ndithu kuti mphunzitsi wopereweredwayu azinka nasaka njira zina zopezera ndalama poonjezera pa malipiro ake.
Nchifukwa chake nthawi yoyenera kuti aphuzitse, ena amakhala akuthamangitsa bizinezi.
Chachiwiri, pazifukwa zosadziwika bwino aphunzitsi kawirikawiri amachedwa kulandira malipiro awo.
Pofika Lachitatu lapitali, pa 3 Julaye, aphunzitsi ena adali asadalandire salale yawo yochepa ndikaleyo.
Aka si koyamba kuti malipiro a phunzitsi achedwe. Nthawi zina masabata amadutsa malipiro a aphuzitsi asakuoneka.
Aphunzitsi afika pozolowera kuchedwaku kotero kuti akalandira munthawi yake ndalama, amadabwa.
Kodi timati aphunzitsiwa azikhala bwanji? Nkale lija aphunzitsi adayamba kudandaula za kuchedwa kwa malipiro. Nchifukwa chiyani boma likulephera kupeza njira yoti mwezi ukamatha malipiro azikhala atakonzedwa? Chikondi cha nkhwangwachomayembekeza ntchito yapamwamba kuchokera kwa aphunzitsi pamene mwezi ukatha sakulabadiridwanchosathandiza.
Ndi chifukwa chake aphunzitsi adatulukira njira yogwira ntchito molingana ndi momwe owalemba ntchito akuwasamalira.
Opwetekeka si aphunzitsi kapena owakonzera malipiro, koma ana omwe sakusulidwa moyenera. Mapeto ake dziko lathu likhalabe lotsalira chifukea nzika zomwe zikudutsa msukulu za bomazi zikhala zosaphunzira moyenera.
Mmalo moloza aphunzitsi, tiloze pomwe pakuyambira vutondondomeko zogwirira ntchito za aphunzitsi nzosakoma konse, ndipo mpovuta kuti aphunzitsi asinthe ngati izi sizikonzedwa.
| 2 |
Subsets and Splits